Categories
MIKA

MIKA 5

1 Uzisonkhana tsopano magulumagulu, mwana wamkazi wa magulu iwe; watimangira misasa, adzapanda woweruza wa Israele ndi ndodo patsaya.

Aneneratu za kubadwa kwa woweruza mu Israele

2 Koma iwe, Betelehemu Efurata, ndiwe wamng’ono kuti ukhale mwa zikwi za Yuda, mwa iwe mudzanditulukira wina wakudzakhala woweruza mu Israele; matulukiro ake ndiwo a kale lomwe, kuyambira nthawi yosayamba.

3 Chifukwa chake Iye adzawapereka kufikira nthawi yoti wobalayo wabala; pamenepo otsala a abale ake adzabwera pamodzi ndi ana a Israele.

4 Ndipo adzaimirira, nadzadyetsa nkhosa zake mu mphamvu ya Yehova, mu ukulu wa dzina la Yehova Mulungu wake; ndipo iwo adzakhalabe; pakuti pamenepo Iye adzakhala wamkulu kufikira malekezero a dziko lapansi.

5 Ndipo ameneyo adzakhala mtendere; pamene a ku Asiriya adzalowa m’dziko lathu, ndi pamene adzaponda m’zinyumba zathu, tidzawaukitsira abusa asanu ndi awiri, ndi akalonga asanu ndi atatu.

6 Ndipo iwo adzatha dziko la Asiriya ndi lupanga, ndi dziko la Nimirodi, ndilo polowera pake; ndipo adzatilanditsa kwa a ku Asiriya pamene alowa m’dziko lathu, pamene aponda m’kati mwa malire athu.

7 Ndipo otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu, ngati mame ochokera kwa Yehova ngati mvula paudzu, yosachedwera munthu, yosalindira ana a anthu.

8 Ndipo otsala a Yakobo adzakhala mwaamitundu, pakati pa mitundu yambiri ya anthu, ngati mkango mwa nyama zakuthengo, ngati msona wa mkango mwa magulu a nkhosa; umenewo ukapitako, upondereza, numwetula, ndipo palibe wakupulumutsa.

9 Dzanja lako likwezeke pamwamba pa iwo akuyambana nawe, ndi adani ako onse aonongeke.

10 Ndipo kudzachitika tsiku ilo, ati Yehova, ndidzaononga akavalo ako m’kati mwako, ndi kutha magaleta ako;

11 ndipo ndidzaononga mizinda ya m’dziko lako, ndi kupasula malinga ako onse;

12 ndipo ndidzaononga zanyanga za m’dzanja lako; ndipo sudzakhalanso nao alosi;

13 ndidzaononganso mafano ako osema, ndi zoimiritsa zako pakati pako; ndipo sudzalambiranso ntchito za manja ako.

14 Ndipo ndidzazula zifanizo zako m’kati mwako, ndi kutha mizinda yako.

15 Ndipo ndidzabwezera amitundu osamvera chilango mu mkwiyo waukali.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MIC/5-0ec30371f0ae0a7cdc9963307c21cf90.mp3?version_id=1068—

Categories
MIKA

MIKA 6

Mulungu atsutsana ndi anthu ake chifukwa cha zoipa zao

1 Tamverani tsono chonena Yehova: Nyamuka, tsutsana nao mapiri, ndi zitunda zimve mau ako.

2 Tamverani, mapiri inu, chitsutsano cha Yehova, ndi inu maziko olimba a dziko lapansi; pakuti Yehova ali nacho chitsutsano ndi anthu ake, ndipo adzatsutsana ndi Israele.

3 Anthu anga inu, ndakuchitirani chiyani? Ndakulemetsani ndi chiyani? Chitani umboni wonditsutsa.

4 Pakuti ndinakukwezani kukutulutsani m’dziko la Ejipito, ndi kuombola inu m’nyumba ya ukapolo; ndipo ndinatuma akutsogolereni Mose, Aroni, ndi Miriyamu.

5 Anthu anga, kumbukiranitu chofunsira Balaki mfumu ya Mowabu, ndi chomuyankha Balamu mwana wa Beori, kuyambira ku Sitimu kufikira ku Giligala; kuti mudziwe zolungama za Yehova.

6 Ndidzafika kwa Yehova ndi chinai, ndi kuwerama kwa Mulungu Wam’mwamba? Kodi ndifike kwa Iye ndi nsembe zopsereza, ndi anaang’ombe a chaka chimodzi?

7 Kodi Yehova adzakondwera nazo nkhosa zamphongo zikwi, kapena ndi mitsinje ya mafuta zikwi khumi? Kodi ndipereke mwana wanga woyamba chifukwa cha kulakwa kwanga, chipatso cha thupi langa chifukwa cha kuchimwa kwa moyo wanga?

8 Iye anakuuza, munthuwe, chomwe chili chokoma; ndipo Yehova afunanji nawe koma kuti uchite cholungama, ndi kukonda chifundo ndi kuyenda modzichepetsa ndi Mulungu wako.

9 Mau a Yehova aitana mzinda, ndi wanzeru aopa dzina lanu; tamverani ndodo, ndi Iye amene anaiika.

10 Kodi m’nyumba ya woipa mukali chuma chosalungama, ndi muyeso wochepa umene ayenera kuipidwa nao?

11 Kodi ndikhoza kuyera ndi miyeso yoipa, ndi thumba la miyala yonyenga?

12 Pakuti anthu ake olemera adzala ndi chiwawa, ndi okhalamo amanena bodza, ndi lilime lao limachita monyenga m’kamwa mwao.

13 Chifukwa chake Inenso ndakukantha ndi kukupweteketsa; ndakupulula chifukwa cha zochimwa zako.

14 Udzadya koma osakhuta; ndi njala yako idzakhala pakati pako; ndipo udzachotsa koma osalanditsa; ndi ichi wachilanditsa ndidzachipereka kulupanga.

15 Udzafesa koma osacheka; udzapondaazitonakoma osadzola mafuta; udzaponda mphesa koma osamwa vinyo.

16 Pakuti asunga malemba a Omuri, ndi ntchito za nyumba ya Ahabu, ndipo mumayenda mu uphungu wao; kuti ndikusandulize bwinja, ndi okhalamo chotsonya; ndipo mudzasenza chitonzo cha anthu anga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MIC/6-9c401742239e12ba75a0b48e74239333.mp3?version_id=1068—

Categories
MIKA

MIKA 7

Za kuipa kwakukulu kwa Aisraele, ndi chifundo cha Mulungu

1 Kalanga ine! Pakuti ndikunga atapulula zipatso za m’mwamvu, atakunkha m’munda wampesa; palibe mphesa zakudya; moyo wanga ukhumba nkhuyu yoyamba kupsa.

2 Watha wachifundo m’dziko, palibe woongoka mwa anthu; onsewo alalira mwazi; yense asaka mbale wake ndi ukonde.

3 Manja ao onse awiri agwira choipa kuchichita ndi changu; kalonga apempha, ndi woweruza aweruza chifukwa cha mphotho; ndi wamkuluyo angonena chosakaza moyo wake; ndipo achiluka pamodzi.

4 Wokoma wa iwo akunga mitungwi; woongoka wao aipa koposa mpanda waminga; tsiku la alonda ako la kulangidwa kwako lafika, tsopano kwafika kuthedwa nzeru kwao.

5 Musakhulupirira bwenzi, musatama bwenzi loyanja; usamtsegulire pakhomo pakamwa pako, ngakhale kwa iye wogona m’fukato mwako.

6 Pakuti mwana wamwamuna apeputsa atate, mwana wamkazi aukira amake, mpongozi aukira mpongozi wake; adani ake a munthu ndiwo a m’nyumba yake.

7 Koma ine, ndidzadikira Yehova; ndidzalindirira Mulungu wa chipulumutso changa; Mulungu wanga adzandimvera.

8 Usandiseka, mdani wangawe; pakugwa ine ndidzaukanso; pokhala ine mumdima Yehova adzakhala kuunika kwanga.

9 Ndidzasenza mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndamchimwira, mpaka andinenera mlandu wanga, ndi kundiweruzira mlandu wanga; adzanditulutsira kwa kuunika, ndipo ndidzapenya chilungamo chake.

10 Pamenepo mdani wanga adzachiona, ndi manyazi adzamkuta iye amene adati kwa ine, Ali kuti Yehova Mulungu wako? Maso anga adzamuona; tsopano adzampondereza ngati thope la m’miseu.

11 Tsiku lakumanga malinga ako, tsiku lomwelo lembalo lidzachotsedwa kunka kutali.

12 Tsiku lomwelo adzadza kwa iwe, kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Ejipito, kuyambira ku Ejipito kufikira ku Mtsinje, ndi kuyambira kunyanja kufikira kunyanja, ndi kuyambira kuphiri kufikira kuphiri.

13 Koma dziko lidzakhala labwinja chifukwa cha iwo okhalamo, mwa zipatso za machitidwe ao.

14 Mudyetse anthu anu ndi ndodo yanu, nkhosa za cholowa chanu zokhala pazokha m’nkhalango pakati pa Karimele, zidye mu Basani ndi mu Giliyadi masiku a kale lomwe.

15 Monga masiku a kutuluka kwako m’dziko la Ejipito ndidzamuonetsa zodabwitsa.

16 Amitunduadzaona nadzachita manyazi ndi mphamvu yao yonse; adzagwira pakamwa, m’makutu mwao mudzagontha.

17 Adzanyambita fumbi ngati njoka; ngati zokwawa za padziko, adzanjenjemera potuluka m’ngaka mwao; adzafika kwa Yehova Mulungu wao ndi mantha, nadzaopa chifukwa cha iwe.

18 Ndani Mulungu wofanana ndi Inu, wakukhululukira mphulupulu, wakupitirira zolakwa za otsala a cholowa chake? Sasunga mkwiyo wake kunthawi yonse popeza akondwera nacho chifundo.

19 Adzabwera, nadzatichitira nsoni; adzagonjetsa mphulupulu zathu; ndipo mudzataya zochimwa zao zonse m’nyanja yakuya.

20 Mudzapatsa kwa Yakobo choonadi, ndi kwa Abrahamu chifundo chimene munalumbirira makolo athu kuyambira masiku a kale lomwe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MIC/7-0919be8687bc3cbebb193b4e6b7c45ee.mp3?version_id=1068—

Categories
NAHUMU

NAHUMU Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli ndi ndakatulo yokondwerera kupasuka kwa Ninive, mzinda waukulu wa Aasiriya amene ankazunza Aisraele kuyambira kale. Kupasuka kwa mzindawo kuwoneka ngati chilango cha Mulungu chogwera anthu onyada ndi ankhanza.

Za mkatimu

Chauta aimba Ninive mlandu

1.1-15

Kupasuka kwa mzindawo

2.1—3.19

Categories
NAHUMU

NAHUMU 1

Chilungamo ndi chifundo cha Mulungu. Adzaononga adani ndi kulanditsa anthu ake

1 Katundu wa Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

2 Yehova ndiye Mulungu wansanje, nabwezera chilango; Yehova ndiye wobwezera chilango, ndi waukali ndithu; Yehova ndiye wobwezera chilango oyambana naye, nasungira mkwiyo pa adani ake.

3 Yehova ndiye wolekerera mkwiyo, koma wa mphamvu yaikulu; ndi wosamasula ndithu wopalamula; njira ya Yehova ili m’kamvulumvulu ndi mumkuntho; ndipo mitambo ndiyo fumbi la mapazi ake.

4 Adzudzula nyanja, naiphwetsa, naumitsa mitsinje yonse; Basani ndi Karimele afota, ndi duwa la ku Lebanoni linyala.

5 Mapiri agwedezeka chifukwa cha Iye, ndi zitunda zisungunuka; ndi dziko lapansi likwezeka pamaso pake, ndi maiko ndi onse okhala m’mwemo.

6 Adzaima ndani pa kulunda kwake? Ndipo adzakhalitsa ndani pa mkwiyo wake wotentha? Ukali wake utsanulidwa ngati moto, ndi matanthwe asweka ndi Iye.

7 Yehova ali wabwino, ndiye polimbikirapo tsiku la msauko; ndipo adziwa iwo omkhulupirira Iye.

8 Koma ndi chigumula chosefukira adzatha konse malo ake, nadzapirikitsira adani ake kumdima.

9 Mulingaliranji chotsutsana ndi Yehova? Iye adzatha psiti; nsautso siidzauka kawiri.

10 Pakuti chinkana akunga minga yoyangayanga, naledzera nacho choledzeretsa chao, adzathedwa konse ngati chiputu chouma.

11 Mwa iwe watuluka wina wolingalira choipa chotsutsana ndi Yehova, ndiye phungu wopanda pake.

12 Atero Yehova: Angakhale iwo ali ndi mphamvu yokwanira, nachuluka momwemo, koma momwemonso adzasalikidwa, ndipo iye adzapitiratu. Chinkana ndakuzunza iwe, sindidzakuzunzanso.

13 Koma tsopano ndidzathyola ndi kukuchotsera goli lake, ndipo ndidzadula zomangira zako.

14 Ndipo Yehova walamulira za iwe kuti asabzalidwenso ena a dzina lako; m’nyumba ya milungu yako ndidzachotsa fano losema ndi fano loyenga; ndidzakukonzerapo manda, pakuti iwe ndiwe wopepuka.

15 Taonani pamapiri mapazi a iye wakulalikira uthenga wabwino, wakubukitsa mtendere! Chita chikondwerero chako, Yuda, kwaniritsa zowinda zako; pakuti wopanda pakeyo sadzapitanso mwa iwe; iye waonongeka konse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NAM/1-9e429d61b8c465db9f9a40f9abc7a2ae.mp3?version_id=1068—

Categories
NAHUMU

NAHUMU 2

Ninive amangidwa misasa nalandidwa

1 Wophwanyayo wakwera pamaso pako; sunga linga, yang’anira panjira, limbitsa m’chuuno mwako, limbikitsatu mphamvu yako.

2 Pakuti Yehova abwezeranso ukulu wake wa Yakobo ngati ukulu wake wa Israele; pakuti okhuthula anawakhuthula, naipsa nthambi zake za mpesa.

3 Zikopa za amphamvu ake zasanduka zofiira, ngwazi zivala mlangali; magaleta anyezimira ndi chitsulo tsiku la kukonzera kwake, ndi mikondo itinthidwa.

4 Magaleta achita mkokomo m’miseu, akankhana m’makwalala; maonekedwe ao akunga miuni, athamanga ngati mphezi.

5 Akumbukira omveka ake; akhumudwa m’kupita kwao, afulumira kulinga lake, ndi chotchinjiriza chakonzeka.

6 Pa zipata za mitsinje patseguka, ndi chinyumba chasungunuka.

7 Chatsimikizika, avulidwa, atengedwa, adzakazi ake alira ngati mau a nkhunda, nadziguguda pachifuwa pao.

8 Koma Ninive wakhala chiyambire chake ngati thamanda lamadzi; koma athawa. Imani, Imani! Ati, koma palibe wocheuka.

9 Funkhanisiliva, funkhani golide; pakuti palibe kutha kwake kwa zosungikazo, kwa chuma cha zipangizo zofunika zilizonse.

10 Ndiye mopanda kanthu mwakemo ndi mwachabe, ndi wopasuka; ndi mtima usungunuka, ndi maondo aombana, ndi m’zuuno zonse muwawa, ndi nkhope zao zatumbuluka.

11 Ili kuti ngaka ya mikango, ndi podyera misona ya mikango, kumene mkango, waumuna ndi waukazi, ukayenda ndi mwana wa mkango, kopanda wakuiposa?

12 Mkangowo unamwetula zofikira ana ake, nusamira yaikazi yake, nudzaza mapanga ake ndi nyama, ngaka zake ndi zojiwa.

13 Taona, nditsutsana nawe, ati Yehova wa makamu, ndipo ndidzatentha magaleta ake mu utsi; ndi lupanga lidzadya misona yako ya mkango; ndipo ndidzachotsa zofunkha zako padziko lapansi, ndi mau a mithenga yako sadzamvekanso.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NAM/2-a3ae7af6dcbd71c31d97042bb6690d10.mp3?version_id=1068—

Categories
NAHUMU

NAHUMU 3

Zoipa za Ninive ndi kupasuka kwake

1 Tsoka mzinda wa mwazi! Udzala nao mabodza ndi zachifwamba; zachifwamba sizidukiza.

2 Kumveka kwa chikoti, ndi mkokomo wa kuyenda kwa njinga za magaleta; ndi kaphatakaphata wa akavalo, ndi gwegwegwe wa magaleta;

3 munthu wokwera pa kavalo, ndi lupanga lonyezimira, ndi mkondo wong’anipa; ndi aunyinji ophedwa, ndi chimulu cha mitembo, palibe kutha zitanda; angokhumudwa ndi zitanda;

4 chifukwa cha chiwerewere chochuluka cha wachiwerewere wokongola, ndiye mkaziyo mwini nyanga, wakugulitsaamitundumwa chiwerewere chake, ndi mabanja mwa nyanga zake.

5 Taona, nditsutsana nawe, ati Yehova wa makamu, ndidzaphimba nkhope yako ndi nsalu yako yoyesa mthendene; ndipo ndidzaonetsa amitundu umaliseche wako, ndi mafumu manyazi ako.

6 Ndipo ndidzakuponyera zonyansa, ndi kukuchititsa manyazi, ndi kukuika chopenyapo.

7 Ndipo kudzali kuti onse akupenyerera iwe adzakuthawa, nadzati, Ninive wapasuka, adzamlira maliro ndani? Ndidzakufunira kuti akukutonthoza?

8 Kodi uli wabwino woposa No-Amoni, wokhala pakati pamtsinje wozingidwa ndi madzi; amene tchemba lake ndilo nyanja, ndi linga lake ndilo nyanja?

9 Kusi ndi Ejipito ndiwo mphamvu yake, ndiyo yosatha, Puti ndi Libiya ndiwo akukuthandiza.

10 Koma iye anatengedwa, analowa ndende; ana ake a makanda anaphwanyika polekeza pake pa miseu yake yonse; ndi pa omveka ake anachita maere, ndi akulu ake onse anamangidwa maunyolo.

11 Iwenso udzaledzera, udzabisala; iwenso udzafunanso polimbikira chifukwa cha mdani.

12 Malinga ako onse adzanga mikuyu ndi nkhuyu zoyamba kupsa; akagwedeza zingokugwa m’kamwa mwa wakudya.

13 Taona, anthu ako m’kati mwako akunga akazi, zipata za dziko lako zatsegulidwira adani ako papakulu; moto watha mipingiridzo yako.

14 Udzitungiretu madzi a nthawi yokumangira misasa, limbikitsa malinga ako, lowa kuthope, ponda dothi, limbitsa ng’anjo yanjerwa.

15 Pomwepo moto udzatha iwe; lupanga lidzakuononga; lidzatha iwe ngati chirimamine; udzichulukitse ngati chirimamine, udzichulukitse ngati dzombe.

16 Wachulukitsa amalonda ako koposa nyenyezi za kuthambo; chirimamine anyambita, nauluka, nathawa.

17 Ovala korona ako akunga dzombe, ndi akazembe, ndi akazembe ako ngati ziwalamsatsi zakutera m’matchinga tsiku lachisanu, koma likatuluka dzuwa ziuluka ndi kuthawa, ndi kumene zinakhalako sikudziwikanso.

18 Abusa ako aodzera, mfumu ya ku Asiriya; omveka ako apumula; anthu ako amwazika pamapiri, ndipo palibe wakuwasonkhanitsa.

19 Palibe chakulunzitsa kuthyoka kwako; bala lako liwawa; onse akumva mbiri yako akuombera manja; pakuti ndaniyo kuipa kwako sikunampitapitabe?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NAM/3-3ee4e47dfc76afa9f7c724171064fb7f.mp3?version_id=1068—

Categories
HABAKUKU

HABAKUKU Mau Oyamba

Mau Oyamba

Mneneriyu adalalika mau ake pamene Ababiloni adaononga ufumu wa Aasiriya (610-600 BC.). Habakuku akhumudwa poona kuti nawonso ndi anthu ankhanza. Iye anavutika mumtima ndipo anadandaula kwa Mulungu nati, “mupenyereranji iwo akuchita mochenjerera, ndi kukhala chete pamene woipa ammeza munthu wolungama woposa iye mwini” (1.13). Yankho la Mulungu ndi lakuti iye adzachitapo kanthu nthawi itakwana, koma pakadali pano, “wolungama adzakhala ndi moyo mwa chikhulupiriro chake” (2.4).

Kwinako bukuli likumaliza ndi ndakatulo yotamanda ukulu wa Mulungu ndi kuonetsa chikhulupiriro chosagwedezeka cha mlakatuliyo.

Za mkatimu

Kudandaula kwa Habakuku

1.1—2.4

Tsoka kwa anthu osalungama

2.5-20

Pemphero la Habakuku

3.1-19

Categories
HABAKUKU

HABAKUKU 1

Chisalungamo cha Ayuda. Ababiloni adzawadzera ndi kuononga zonse. Mneneri apempherera Ayuda

1 Katundu adamuonamneneriHabakuku

2 Yehova, ndidzafuula mpaka liti osamva Inu? Ndifuulira kwa Inu za chiwawa, koma simupulumutsa.

3 Mundionetseranji zopanda pake, ndi kundionetsa zovuta? Pakuti kufunkha ndi chiwawa zili pamaso panga; ndipo pali ndeu, nauka makani.

4 Pakuti chilamulo chalekeka, ndi chiweruzo sichitulukira konse; popeza woipa azinga wolungama, chifukwa chake chiweruzo chituluka chopindika.

5 Penyani mwaamitundu, penyetsetsani, nimudabwe kwakukulu, pakuti ndichita ntchito masiku anu, imene simudzavomera chinkana akufotokozerani.

6 Pakuti taonani, ndiukitsa Ababiloni, mtundu uja wowawa ndi waliwiro, wopitira pa chitando cha dziko lapansi, kulowa m’malo mosati mwao, mukhale mwaomwao.

7 Ali oopsa, achititsa mantha, chiweruzo chao ndi ukulu wao zituluka kwa iwo eni.

8 Akavalo ao aposa anyalugwe liwiro lao, aposa mimbulu ya madzulo ukali wao, ndipo apakavalo ao atanda; inde apakavalo ao afumira kutali; auluka ngati chiombankhanga chofulumira kudya.

9 Adzera chiwawa onsewo; nkhope zao zikhazikika zolunjika m’tsogolo; asonkhanitsa andende ngati mchenga.

10 Inde anyoza mafumu, aseka akalonga; aseka linga lililonse; popeza aunjika dothi, nalilanda.

11 Pamenepo adzapitirira ngati mphepo, nadzalakwa ndi kupalamula, iye amene aiyesa mphamvu yake mulungu wake.

12 Si ndinu wachikhalire, Yehova Mulungu wanga, wopatulika wanga? Sitidzafa. Yehova munamuikiratu kuti aweruzidwe; ndipo Inu, Thanthwe, munamkhazika kuti alangidwe.

13 Inu wa maso osalakwa, osapenya choipa, osakhoza kupenyerera chovuta, mupenyereranji iwo akuchita mochenjerera, ndi kukhala chete pamene woipa ammeza munthu wolungama woposa iye mwini;

14 ndi kuyesa anthu ngati nsomba za m’nyanja, ngati zokwawa zopanda wakuzilamulira.

15 Aziwedza zonse ndi mbedza, azigwira mu ukonde wake, nazisonkhanitsa m’khoka mwake; chifukwa chake asekera nakondwerera.

16 Chifukwa chake aphera nsembe ukonde wake, nafukizira khoka lake, pakuti mwa izi gawo lake lilemera, ndi chakudya chake chichuluka.

17 Kodi m’mwemo adzakhuthula mu ukonde mwake osaleka kuphabe amitundu?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HAB/1-db82ab5beb63c7e08ff3f5ffd53ba4b0.mp3?version_id=1068—

Categories
HABAKUKU

HABAKUKU 2

Ababiloni omwe adzalangidwa

1 Ndidzaima pa dindiro langa ndi kudziika palinga, ndipo ndidzayang’anira ndione ngati adzanenanji mwa ine, ngatinso ndidzamyankha chiyani pa choneneza changa.

2 Ndipo Yehova anandiyankha nati, Lembera masomphenyawo, nuwachenutse pamagome, kuti awawerenge mofulumira.

3 Pakuti masomphenyawo alindira nyengo yoikidwiratu, ndipo afulumirira potsirizira pake, osanama; akachedwa uwalindirire; popeza afika ndithu, osazengereza.

4 Taonani, moyo wake udzikuza, wosaongoka m’kati mwake; koma wolungama adzakhala ndi moyo mwa chikhulupiriro chake.

5 Ndiponso vinyo ngwonyenga, ngati munthu wodzikuza, wosakhala kwao; wakukulitsa chikhumbo chake ngati kunsi kwa manda, akunga imfa, yosakhuta, koma adzisonkhanitsiraamitunduonse, nadzimemezera mitundu yonse ya anthu.

6 Kodi sadzamnenera fanizo onsewo, ndi mwambi womnyodola, ndi kuti, Tsoka iye wochulukitsa zimene sizili zake? Mpaka liti? Iye wodzisenzera zigwiriro.

7 Sadzauka kodi modzidzimuka iwo amene adzakuluma, ndi kugalamuka iwo amene adzakugwedezetsa; ndipo udzakhala zofunkha zao?

8 Popeza iwe wafunkha amitundu ambiri, otsala onse a mitundu ya anthu adzakufunkha iwe; chifukwa cha mwazi wa anthu, ndi chiwawa chochitikira dziko, mzinda, ndi onse okhalamo.

9 Tsoka iye wakupindulitsira nyumba yake phindu loipa, kuti aike chisanja chake ponyamuka, kuti alanditsidwe m’dzanja la choipa!

10 Wapangira nyumba yako chamanyazi, pakuononga mitundu yambiri ya anthu, ndipo wachimwira moyo wako.

11 Pakuti mwala wa m’khoma ufuula, ndi mtanda wa kuphaso udzauvomereza.

12 Tsoka iye wakumanga mzinda ndi mwazi, nakhazikitsa mzinda ndi chisalungamo!

13 Taonani, sichichokera kwa Yehova wa makamu kodi kuti mitundu ya anthu ingogwirira moto ntchito, ndi anthu angodzilemetsa pa zopanda pake?

14 Pakuti dziko lapansi lidzadzazidwa ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga madzi amphimba pansi pa nyanja.

15 Tsoka wakuninkha mnzake chakumwa, ndi kuonjezako mankhwala ako, ndi kumledzeretsa, kuti upenyerere manyazi ao!

16 Udzazidwa nao manyazi m’malo mwa ulemerero; imwa iwenso, nukhale wosadulidwa; chikho cha dzanja lamanja la Yehova chidzatembenukira iwe, ndi kusanza kwa manyazi kudzakhala pa ulemerero wako.

17 Pakuti chiwawa chidachitikira Lebanoni chidzakukuta, ndi chionongeko cha nyama chidzakuopsa; chifukwa cha mwazi wa anthu, ndi chiwawa chochitidwira dziko, mzinda, ndi onse okhalamo.

18 Apindulanji nalo fano losema, kuti wakulipanga analisema; fano loyenga ndi mphunzitsi wamabodza, kuti wakulipanga alikhulupirira, atapanga mafano osanena mau?

19 Tsoka iye wakunena kwa mtengo, Galamuka; ndi kwa mwala wosalankhula, Nyamuka! Kodi ichi chiphunzitsa? Taona chakutidwa ndi golide ndisiliva, ndi m’kati mwake mulibe mpweya konse.

20 Koma Yehova ali mu Kachisi wake wopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HAB/2-a7456691eb67bc77a4a5c326a52c01ea.mp3?version_id=1068—