Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 43

Kukonzekanso kwa Kachisi: ulemerero wa Mulungu

1 Pamenepo anamuka nane kuchipata choloza kum’mawa,

2 ndipo taonani, ulemerero wa Mulungu wa Israele unadzera njira ya kum’mawa, ndi mau ake ananga mkokomo wa madzi ambiri, ndi dziko linanyezimira ndi ulemerero wake.

3 Ndipo maonekedwe a masomphenya ndinawaona anali monga masomphenya aja ndinawaona pakudza ine kupasula mzinda; ndi masomphenyawa anali ngati masomphenya aja ndinawaona kumtsinje wa Kebara; ndipo ndinagwa nkhope pansi.

4 Ndipo ulemerero wa Yehova unalowa mu Kachisi kudzera njira ya chipata choloza kum’mawa.

5 Ndipo mzimu unandinyamula numuka nane kubwalo la m’kati; ndipo taonani, ulemerero wa Yehova unadzaza Kachisi.

6 Ndipo ndinamva wina alikulankhula nane ali mu Kachisi, naima nane munthu.

7 Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, pano mpokhala mpando wachifumu wanga, mpoponda kumapazi anga, pomwe ndidzakhala pakati pa ana a Israele kosatha; ndi nyumba ya Israele siidzadetsanso dzina langa loyera, ngakhale iwo kapena mafumu ao, mwa chigololo chao, ndi mitembo ya mafumu ao pa misanje yao,

8 ndi kuika chiundo chao pafupi pa chiundo changa, ndi mphuthu yao pa mbali ya mphuthu yanga, ndipo panali khoma lokha pakati pa iwo ndi Ine, nadetsa dzina langa loyera ndi zonyansa zao anazichita; chifukwa chake ndinawatha mu mkwiyo wanga.

9 Ataye tsono chigololo chao ndi mitembo ya mafumu ao kutali kwa Ine, ndipo ndidzakhala pakati pao kosatha.

10 Wobadwa ndi munthu iwe, onetsa nyumba ya Israele Kachisiyu, kuti achite manyazi ndi mphulupulu zao; ndipo ayese muyeso wake.

11 Ndipo ngati akachita manyazi nazo zonse anazichita, uwadziwitse maonekedwe a Kachisiyu, ndi muyeso wake, ndi potulukira pake, ndi polowera pake, ndi malongosoledwe ake onse, ndi malemba ake onse, ngakhale maonekedwe ake onse, ndi malamulo ake onse; nuwalembere pamaso pao, kuti asunge maonekedwe ake onse, ndi malemba ake onse, nawachite.

12 Lamulo la Kachisi ndi ili: pamwamba paphiri malire ake onse pozungulira pake azikhala opatulika kwambiri. Taonani, limeneli ndi lamulo la Kachisi.

13 Ndipo miyeso ya guwa la nsembe, kuyesa mikono ndi iyi: (mkonowo ndiwo mkono ndi chikhato), tsinde lake likhale mkono, ndi kupingasa kwake dzanja limodzi, ndi mkuzi wake m’mphepete mwake pozungulira pake kuyesa zala; ili ndi tsinde la guwali.

14 Ndi kuyambira kunsi kwake kunthaka, kufikira phaka lamunsi, mikono iwiri; ndi kupingasa kwake mkono umodzi; ndi kuyambira phaka laling’ono kufikira phaka lalikulu mikono inai; ndi kupingasa kwake mkono.

15 Ndi guwa lapamwamba mikono inai; ndi pamoto paguwa padzatuluka nyanga zinai.

16 Ndi pamoto paguwa, m’litali mwake mikono khumi ndi iwiri, ndi kupingasa kwake khumi ndi iwiri, laphwamphwa mbali zake zinai.

17 Ndi phaka, m’litali mwake mikono khumi ndi inai, ndi kupingasa kwake mikono khumi ndi inai kumbali zake zinai; ndi mkuzi wake pozungulira pake mkono wa nusu, ndi tsinde lake mkono pozungulira pake, ndi makwerero ake aloza kum’mawa.

18 Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, atero Ambuye Yehova, Malemba a guwa la nsembe, tsiku lakulimanga, kuperekapo nsembe zopsereza, ndi kuwazapo mwazi, ndi awa;

19 Upatse ansembe Alevi, a mbeu za Zadoki, okhala pafupi ndi Ine, kunditumikira Ine, ati Ambuye Yehova, mwanawang’ombe, akhale wa nsembe yauchimo.

20 Nutengeko mwazi wake, ndi kupaka pa nyanga zinai za guwa, ndi pangodya zinai za phaka, ndi pa mkuzi wake pozungulira; motero uliyeretse ndi kulichitira chotetezera.

21 Utengenso ng’ombe ya nsembe yauchimo, aipsereze pamalo oikika a Kachisi kunja kwa malo opatulika.

22 Ndipo tsiku lachiwiri upereke tonde wopanda chilema, akhale nsembe yauchimo; ndipo ayeretse guwa la nsembe monga umo analiyeretsera ndi ng’ombeyo.

23 Utatha kuliyeretsa upereke mwanawang’ombe wopanda chilema, ndi nkhosa yamphongo ya zoweta yopanda chilema.

24 Ndipo ubwere nazo kwa Yehova, ndi ansembe athirepo mchere, ndi kuzipereka nsembe yopsereza ya Yehova.

25 Masiku asanu ndi awiri uzikonzera mbuzi tsiku ndi tsiku, ikhale nsembe yauchimo; akonzerenso mwanawang’ombe, ndi nkhosa yamphongo ya zoweta zopanda chilema.

26 Masiku asanu ndi awiri achite chotetezera guwali ndi kuliyeretsa, momwemo alipatule.

27 Ndipo atatsiriza masiku, kudzachitika tsiku lachisanu ndi chitatu ndi m’tsogolo, ansembe azichita nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zanu zoyamika paguwalo; ndipo ndidzakulandirani, ati Ambuye Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/43-e77b8c498a090a08716e1505fe587e3d.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 44

Kukonzekanso kwa Kachisi utumiki wa Alevi ndi ansembe

1 Pamenepo anandibweza njira ya kuchipata chakunja cha malo opatulika choloza kum’mawa, koma chinatsekedwa.

2 Ndipo Yehova anati kwa ine, Chipata ichi chitsekeke, chisatseguke, osalowako munthu; pakuti Yehova Mulungu wa Israele walowerapo; chifukwa chake chitsekeke.

3 Koma kunena za kalonga, iye akhale m’menemo monga kalonga kudya mkate pamaso pa Yehova; alowe kunjira ya kukhonde la chipata, natulukire njira yomweyi.

4 Atatero anamuka nane njira ya chipata cha kumpoto kukhomo kwa Kachisi, ndipo ndinapenya, taonani, ulemerero wa Yehova unadzaza nyumba ya Yehova; pamenepo ndinagwa nkhope pansi.

5 Ndipo Yehova anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, samalira bwino, nupenye ndi maso ako, numve m’makutu mwako zonse ndidzanena nawe, kunena za malemba onse a nyumba ya Yehova, ndi malamulo ake onse; nusamalire bwino malowedwe a nyumbayi, ndi matulukidwe ake onse a malo opatulika.

6 Nunene kwa opandukawo, kwa nyumba ya Israele, Atero Ambuye Yehova, Nyumba ya Israele inu, Zikukoleni zonyansa zanu zonse;

7 popeza mwalowa nao achilendo osadulidwa m’mtima, osadulidwa m’thupi akhale m’malo anga opatulika kuwadetsa, ndiwo nyumba yanga, popereka inu mkate wanga, mafuta, ndi mwazi; ndipo munathyola pangano langa pamodzi ndi zonyansa zanu zonse.

8 Ndipo simunasunge udikiro wa zopatulika zanga, koma mwadziikira nokha osunga udikiro wanga m’malo anga opatulika.

9 Atero Ambuye Yehova, Palibe mlendo wosadulidwa m’mtima, wosadulidwa m’thupi, alowe m’malo anga opatulika, mwa alendo onse ali pakati pa ana a Israele.

10 Koma Aleviwo anandichokera kunka kutaliwo, posokera Israele, amene anandisokerera ndi kutsata mafano ao, iwowa adzasenza mphulupulu yao.

11 Koma adzakhala atumiki m’malo anga opatulika, akuyang’anira kuzipata za Kachisi, ndi kutumikira mu Kachisimo, aziwaphera anthu nsembe yopsereza, ndi nsembe yophera, naime pamaso pao kuwatumikira.

12 Popeza anawatumikira pamaso pa mafano ao, nakhala chokhumudwitsa cha mphulupulu cha nyumba ya Israele, chifukwa chake ndawakwezera dzanja langa, ati Ambuye Yehova; ndipo adzasenza mphulupulu yao.

13 Ndipo asayandikire kwa Ine kundigwirira ntchito ya nsembe, kapena kuyandikira zopatulika zanga zilizonse zopatulika kwambirizo; koma azisenza manyazi ao, ndi zonyansa zao anazichita.

14 Koma ndidzawaika akhale osunga udikiro wa Kachisi kwa utumiki wake wonse, ndi zonse zakumachitika m’mwemo.

15 Koma ansembe Alevi, ana a Zadoki, akusunga udikiro wa malo anga opatulika pondisokerera ana a Israele, iwowa adzandiyandikira kunditumikira Ine, nadzaima pamaso panga, kupereka mafuta ndi mwazi kwa Ine, ati Ambuye Yehova;

16 iwowa adzalowa m’malo anga opatulika, nadzayandikira kugome langa kunditumikira, nadzasunga udikiro wanga.

17 Ndipo kudzatero, polowa iwo kuzipata za bwalo lam’kati avale zovala zabafuta; koma zaubweya asazivale ponditumikira Ine m’zipata za bwalo la m’kati, ndi mu Kachisi.

18 Akhale nao akapa abafuta pamitu pao, ndi akabudula m’chuuno mwao; asavale m’chuuno kanthu kalikonse kakuchititsa thukuta.

19 Ndipo akatulukira kubwalo lakunja, kubwalo lakunja kuli anthu, azivula zovala zao zimene atumikira nazo, naziike m’zipinda zopatulika, navale zovala zina; angapatule anthu ndi zovala zao.

20 Ndipo asamete mitu yao, kapena asalekerere nzera za tsitsi lao zikule, azingoyepula tsitsi la mitu yao.

21 Kungakhale kumwa vinyo, wansembe asamwe polowa kubwalo la m’katimo.

22 Kungakhale kutenga amasiye kapena osudzulidwa akhale akazi ao, asachite; koma atenge anamwali a mbeu ya nyumba ya Israele, kapena wamasiye ndiye wamasiye wa wansembe.

23 Ndipo aziphunzitsa anthu anga asiyanitse pakati pa zopatulika ndi zinthu wamba, ndi kuwazindikiritsa pakati pa zodetsa ndi zoyera.

24 Ndipo pakakhala mlandu, aimeko kuweruza; auweruze monga mwa maweruzo anga, ndipo azisunga malamulo anga, ndi malemba anga, pazikondwerero zanga zonse zoikika; napatulikitsemasabataanga.

25 Ndipo asayandikire kwa munthu aliyense wakufa, angadzidetse; koma chifukwa cha atate, kapena mai, kapena mwana wamwamuna, kapena mwana wamkazi, kapena mbale, kapena mlongo wopanda mwamuna, nkuloleka kudzidetsa.

26 Ndipo atayeretsedwa amwerengere masiku asanu ndi awiri.

27 Ndipo tsiku loti alowa m’malo opatulika, bwalo lam’kati, kutumikira m’malo opatulika, apereke nsembe yake yauchimo, ati Ambuye Yehova.

28 Ndipo adzakhala nacho cholowa; Ine ndine cholowa chao; musawapatsa cholandira chao mu Israele; Ine ndine cholandira chao.

29 Azidya nsembe yaufa, ndi nsembe yauchimo, ndi nsembe yopalamula; ndipo zilizonse zoperekedwa chiperekere mu Israele ndi zao.

30 Ndi zoyamba za zipatso zoyamba za zinthu zilizonse, ndi nsembe zokweza zilizonse za nsembe zanu zonse zokweza nza ansembe; muperekenso ufa wanu woyamba kwa wansembe, kuti mdalitso ukhalebe pa nyumba yako.

31 Ansembe asadyeko kanthu kakufa kokha, kapena kogwidwa ndi chilombo, ngakhale mbalame, kapena nyama.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/44-c3408ef48043d94f88e9515dd8fa00ed.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 45

Chigawo cha dziko

1 Ndipo pogawa dziko likhale cholowa chao, mupereke chopereka kwa Yehova, ndicho gawo lopatulika la dziko; m’litali mwake likhale la mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu, ndi kupingasa kwake mikono zikwi makumi awiri; likhale lopatulika m’malire ake onse pozungulira pake.

2 Kutengako malo opatulika akhale nayo mikono mazana asanu m’litali mwake, ndi mazana asanu kupingasa kwake, laphwamphwa pozungulira pake; ndi pabwalo pake poyera pozungulira pake mikono makumi asanu.

3 Ndipo kuyambira poyesedwapo uyese mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu m’litali mwake, ndi mikono zikwi khumi kupingasa kwake; m’menemo ndimo mukhale malo opatulika, ndiwo opatulika, ndiwo opatulika kwambiri.

4 Ndilo gawo lopatulika la dziko, ndilo la ansembe atumiki a malo opatulika, amene ayandikira kutumikira Yehova; apo ndipo amange nyumba zao, likhale malo a pa okha a kwa malo opatulika.

5 Ndipo mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu m’litali mwake, ndi mikono zikwi khumi kupingasa kwake, ndilo gawo la Alevi, atumiki a Kachisi; likhale laolao la mizinda yokhalamo.

6 Ndipo dziko lake la mzindawo mulipereke la mikono zikwi zisanu kupingasa kwake, ndi mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu m’litali mwake, pa mbali ya chipereko chopatulika, ndilo la nyumba yonse ya Israele.

7 Ndipo kalonga adzakhala nalo gawo lake mbali ina ndi mbali inzake ya chipereko chopatulika, ndi ya dziko la mzinda, kutsogolo kwa chipereko chopatulika, ndi kutsogolo kwa dziko la mzinda, mbali ya kumadzulo, ndi mbali ya kum’mawa; ndi m’litali mwake mudzalingana ndi limodzi la magawo, kuyambira kumalire a kumadzulo kufikira malire a kum’mawa.

8 M’dzikomo ili lidzakhala lakelake mu Israele; ndipo akalonga anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzapereka dziko kwa nyumba ya Israele monga mwa mafuko ao.

9 Atero Ambuye Yehova, Likufikireni akalonga a Israele inu, lekani kuchita chiwawa, ndi kulanda za eni ake; muchite chiweruzo ndi chilungamo; lekani kupirikitsa anthu anga m’zolowa zao, ati Ambuye Yehova.

10 Muzikhala nayo miyeso yoona, ndi efa woona, ndi bati loona.

11 Efa ndi bati zikhale za muyeso umodzi, bati liyese limodzi la magawo khumi la homeri, efa lomwe liyese limodzi la magawo khumi la homeri; muyeso wao uyesedwa monga mwa homeri.

12 Ndipo sekeli ndilo magera makumi awiri; masekeli makumi awiri, ndi masekeli awiri ndi asanu, ndi masekeli khumi ndi asanu, ndiwo muyeso wa mina wanu.

13 Chopereka muchipereke ndicho limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa homeri wa tirigu; muperekenso limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa homeri wa barele;

14 ndi gawo lonenedwa la mafuta, la bati wa mafuta, ndilo limodzi la magawo khumi la bati, kulitapa pa kori; ndiwo mabati khumi, ndiwo homeri; pakuti mabati khumi ndiwo homeri;

15 ndimwanawankhosammodzi wa zoweta, kumtenga pa mazana awiri wochokera kumadimba a Israele, ndiye wa nsembe yaufa, ndi wa nsembe yopsereza, ndi wa nsembe zoyamika, kuwachitira chotetezera, ati Ambuye Yehova.

16 Anthu onse a m’dziko azipereka chopereka ichi chikhale cha kalonga wa mu Israele.

17 Ndipo udindo wa kalonga ndiwo kupereka nsembe zopsereza, ndi nsembe zaufa, ndi nsembe zothira, pachikondwerero, ndi pokhala mwezi, ndi pamasabata; pa zikondwerero zonse zoikika a nyumba ya Israele; ndipo apereke nsembe yauchimo, ndi nsembe yaufa, ndi nsembe yopsereza, ndi nsembe zamtendere, kuchitira chotetezera nyumba ya Israele.

Nsembe ya pa mwezi woyamba

18 Atero Ambuye Yehova, Mwezi woyamba, tsiku loyamba la mwezi, uzitenga mwanawang’ombe wopanda chilema, ndipo uyeretse malo opatulika.

19 Ndipo wansembe atengeko mwazi wa nsembe yauchimo, naupake pa mphuthu za Kachisi, ndi pangodya zinai za phaka la guwa la nsembe, ndi pa mphuthu za chipata cha bwalo lam’kati.

20 Tsiku lachisanu ndi chiwiri la mweziwo uchitire momwemo aliyense wolakwa ndi wopusa; motero muchitire Kachisiyo chomtetezera.

Za Paska

21 Mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi chinai la mwezi, muzichitaPaska, chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri; audye mkate wopanda chotupitsa.

22 Ndipo tsiku lomwelo kalonga adzikonzere yekha ndi anthu onse a m’dziko ng’ombe, ikhale ya nsembe yauchimo.

23 Ndipo masiku asanu ndi awiri a chikondwerero akonzere Yehova nsembe yopsereza, ng’ombe zisanu ndi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri zopanda chilema, tsiku ndi tsiku, masiku asanu ndi awiriwa; ndi tonde tsiku ndi tsiku, akhale wa nsembe yauchimo.

24 Nakonze nsembe yaufa, kung’ombe kukhale efa; ndi kunkhosa yamphongo kukhale efa; ndi kuefa kukhale hini wa mafuta.

25 Mwezi wachisanu ndi chiwiri, tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi, pachikondwerero, achite momwemo masiku asanu ndi awiri, monga mwa nsembe yauchimo, monga mwa nsembe yopsereza, ndi monga mwa nsembe yaufa, ndi monga mwa mafuta.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/45-6758b70849ec027f07a9050379b004e6.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 46

Za Sabata ndi pokhala mwezi

1 Atero Ambuye Yehova, Pa chipata cha bwalo lam’kati choloza kum’mawa patsekedwe masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito; koma tsiku laSabatapatsegulidwe, ndi tsiku lokhala mwezi patsegulidwe.

2 Ndipo kalonga azilowera njira ya kukhonde la chipatacho, kunja kwake, naime kunsanamira ya chipata; ndipo ansembe akonze nsembe yake yopsereza, ndi nsembe zake zoyamika, nalambire iye kuchiundo cha chipata; atatero atuluke; koma pachipata pasatsekedwe mpaka madzulo.

3 Ndipo anthu a m’dziko alambire pa chitseko cha chipata ichi pamaso pa Yehova pamasabata, ndi pokhala mwezi.

4 Ndipo nsembe yopsereza imene kalonga azipereka kwa Yehova pa Sabata ndiyo anaankhosa asanu ndi mmodzi opanda chilema, ndi nkhosa yamphongo yopanda chilema,

5 ndi nsembe yaufa ikhale efa wa pa nkhosa yamphongo, ndi nsembe ya ufa wa pa anaankhosa, monga akhoza kupatsa; ndi hini wa mafuta wa paefa.

6 Ndipo nsembe ya tsiku lokhala mwezi ikhale mwanawang’ombe wopanda chilema, ndi anaankhosa asanu ndi mmodzi, ndi nkhosa yamphongo, zikhale zopanda chilema;

7 ndipo akonze nsembe yaufa, efa wa pa ng’ombe, ndi efa wa pa nkhosa yamphongo, ndi pa anaankhosa, monga akhoza; ndi hini wa mafuta wa paefa.

8 Ndipo polowa kalonga azilowera njira ya kukhonde la chipata, natuluke njira yomweyo.

Malangizo a popereka nsembe

9 Koma pofika anthu a m’dziko pamaso pa Yehova m’zikondwerero zoikika, iye amene alowera njira ya kuchipata cha kumpoto kudzalambira, atulukire njira ya kuchipata cha kumwera; ndi iye amene alowera njira ya kuchipata cha kumwera, atulukire njira ya kuchipata cha kumpoto; asabwerere njira ya chipata anadzeracho, koma atulukire m’tsogolo mwake.

10 Kalongayo tsono, polowa iwo alowe pakati pao, ndipo potuluka iwo atulukire pamodzi.

11 Ndi pazikondwerero, ndi pa masiku opatulika, nsembe yaufa ikhale ya efa wa pa ng’ombe, ndi efa wa pa nkhosa yamphongo, ndi pa anaankhosa, monga akhoza kupatsa; ndi hini wa mafuta wa paefa.

12 Ndipo kalonga akapereka chopereka chaufulu nsembe yopsereza, kapena nsembe zoyamika kwa Yehova, amtsegulire pa chipata choloza kum’mawa; ndipo azipereka nsembe yake yopsereza, ndi nsembe zake zoyamika, monga umo amachitira tsiku la Sabata; atatero atuluke; ndipo atatuluka, wina atseke pachipata.

13 Uziperekanso kwa Yehova mwanawankhosa wa chaka chimodzi akhale nsembe yopsereza wopanda chilema, tsiku ndi tsiku, m’mawa ndi m’mawa, uzimpereka.

14 Uperekenso nsembe yaufa pamodzi naye m’mawa ndi m’mawa, limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, ndi limodzi la magawo atatu la hini wa mafuta, kusakaniza ndi ufa wosalala, ndiyo nsembe yaufa ya Yehova kosalekeza, mwa lemba losatha.

15 Momwemo aperekemwanawankhosa, ndi nsembe yaufa, ndi mafuta, m’mawa ndi m’mawa, nsembe yopsereza kosalekeza.

Mapatsidwe a kalonga

16 Atero Ambuye Yehova, Kalonga akapatsa mwana wake wina wamwamuna mphatso idzakhala cholowa chake, ndicho chaochao cha ana ake, cholowa chao.

17 Koma akapatsa mphatso yotenga kucholowa chake kwa wina wa anyamata ake, idzakhala yake mpaka chaka cha ufulu; pamenepo ibwerere kwa kalonga, koma cholowa chake chikhale cha ana ake.

18 Ndipo kalonga asatengeko cholowa cha anthu kuwazunza, ndi kulanda dziko laolao; apatse ana ake cholowa kulemba dziko lakelake, kuti anthu anga asabalalike, yense kuchoka m’dziko lake.

Pophikira ansembe

19 Pamenepo anapita ndi ine podzera paja pali kumbali ya chipata kunka kuzipinda zopatulika za ansembe zoloza kumpoto; ndipo taonani, kunali malo chauko kumadzulo.

20 Ndipo anati kwa ine, Pano ndipo ansembe aziphikira nsembe yopalamula, ndi nsembe yauchimo; kumenenso aziotcha mikate ya ufa wa nsembe, kuti asatuluke nazo kubwalo lakunja ndi kupatulikitsa anthu.

21 Pamenepo anatulukira nane kubwalo lakunja, nandipititsa kungodya zinai za bwaloli; ndipo taonani, m’ngodya monse munali bwalo.

22 M’ngodya zinai za bwalo munali mabwalo ochingika, m’litali mwake mikono makumi anai, kupingasa kwake makumi atatu; awa anai m’ngodyazi analingana muyeso wake.

23 Ndipo panali maguwa pozungulira pake m’menemo, pozungulira pake pa mabwalo anai; ndipo anamanga maguwawo ndi mafuwa pansi pake pozungulirapo.

24 Ndipo anati kwa ine, Izi ndi nyumba zophikiramo, kumene atumiki a Kachisi aziphikira nsembe ya anthu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/46-9abfe4c06f586fbedee22c91dca9184e.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 47

Masomphenya a madzi otuluka mu Kachisi watsopano

1 Ndipo anandibwezera ku khomo la nyumba, ndipo taonani, panatumphuka madzi pansi pa chiundo cha nyumba kum’mawa; pakuti khomo lake la nyumba linaloza kum’mawa; ndipo madzi anatsika kuchokera pansi pa nyumba, kumbali ya lamanja lake, kumwera kwa guwa la nsembe.

2 Pamenepo anatuluka nane njira ya kuchipata cha kumpoto, nazungulira nane njira yakunja kunka kuchipata chakunja, njira ya kuchipata choloza kum’mawa; ndipo taonani, panatuluka madzi pa mbali ya kulamanja.

3 Potuluka munthuyu kunka kum’mawa ndi chingwe choyesera m’dzanja lake, anayesa mikono chikwi chimodzi, nandipititsa pamadzi, madzi oyesa m’kakolo.

4 Nayesanso chikwi chimodzi, nandipititsa pamadzi, madzi oyesa m’maondo. Nayesanso chikwi chimodzi, nandipititsa pamadzi, madzi oyesa m’chuuno.

5 Atatero anayesanso chikwi chimodzi, ndipo mtsinje wosakhoza kuoloka ine, popeza madzi adakula, madzi osambira, mtsinje wosaoloka munthu.

6 Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, waona ichi? Nanditenga kundikwezetsa ndi mtsinje.

7 Nditabwera tsono, taonani, pa gombe la mtsinjewo mitengo yambirimbiri tsidya lino ndi lija.

8 Pamenepo anati kwa ine, Madzi awa atulukira kudera la kum’mawa, natsikira kuchidikha, nayenda kunyanja; atathira kunyanja akonzeka madzi ake.

9 Ndipo kudzatero kuti zamoyo zonse zochuluka zidzakhala ndi moyo kulikonse mtsinjewo ufikako, ndi nsomba zidzachuluka kwambiri; pakuti madzi awa anafikako, nakonzeka madzi a m’nyanja; ndipo kulikonse mtsinje ufikako zilizonse zidzakhala ndi moyo.

10 Ndipo kudzachitika, kuti asodzi adzaima komweko; kuyambira pa Engedi kufikira ku Enegilaimu kudzakhala poyanikira makoka; nsomba zao zidzakhala za mitundumitundu, ngati nsomba za mu Nyanja Yaikulu, zambirimbiri.

11 Koma pali matope ake ndi zithaphwi zake sipadzakonzeka, paperekedwa pakhale pamchere.

12 Ndipo kumtsinje, kugombe kwake tsidya lino ndi lija, kudzamera mtengo uliwonse wa chakudya, osafota tsamba lake, zipatso zake zomwe zosasowa; idzabala zipatso zatsopano mwezi ndi mwezi, popeza madzi ake atumphuka m’malo opatulika; ndi zipatso zake zidzakhala chakudya, ndi tsamba lake lakuchiritsa.

Malire a dziko

13 Atero Ambuye Yehova, Malire amene mugawe nao dziko likhale cholowa chao monga mwa mafuko khumi ndi awiri a Israele ndi awa: Yosefe akhale nao magawo awiri.

14 Ndipo mudzakhala nalo cholowa chanu wina ndi mnzake yemwe, ndilo limene ndinakwezapo dzanja langa kulipereka kwa makolo anu, ndi dziko ili lidzakugwerani cholowa chanu.

15 Ndipo malire a dzikoli ndi awa: mbali ya kumpoto, kuyambira ku Nyanja Yaikulu, kutsata njira ya ku Hetiloni, kufikira polowera ku Zedadi;

16 Hamati, Berota, Sibraimu, ndiwo pakati pa malire a Damasiko, ndi malire a Hamati; Hazere-Hatikoni ndiwo kumalire a Haurani.

17 Ndi malire ochokera kunyanja ndiwo Hazar-Enoni, kumalire a Damasiko, ndi kumpoto kulinga kumpoto kuli malire a Hamati. Ndiyo mbali ya kumpoto.

18 Ndi mbali ya kum’mawa pakati pa Haurani, ndi Damasiko, ndi Giliyadi, ndi dziko la Israele, ndiwo Yordani; muyese kuyambira malire a kumpoto kufikira nyanja ya kum’mawa. Ndiyo mbali ya kum’mawa.

19 Ndi mbali ya kumwera kuloza kumwera ndiyo kuyambira ku Tamara kufikira ku madzi a Meribati-Kadesi, ku mtsinje wa Ejipito, ndi ku Nyanja Yaikulu. Ndiyo mbali ya kumwera kuloza kumwera.

20 Ndi mbali ya kumadzulo ndiyo Nyanja Yaikulu, kuyambira malire a kumwera kufikira pandunji polowera ku Hamati. Ndiyo mbali ya kumadzulo.

21 Motero mudzigawire dziko ili monga mwa mafuko a Israele.

22 Ndipo kudzachitika kuti muligawe ndi kuchita maere, likhale cholowa chanu, ndi cha alendo akukhala pakati pa inu; ndipo akhale kwa inu ngati obadwa m’dziko mwa ana a Israele, alandire cholowa pamodzi ndi inu mwa mafuko a Israele.

23 Ndipo kudzatero kuti kufuko kumene mlendo akhalako kumeneko mumpatse cholowa chake, ati Ambuye Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/47-d2b89dd125db9b72a1cf11dd99369f0f.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 48

Magawidwe a dziko mwa mafuko khumi ndi awiri

1 Maina a mafuko tsono ndi awa: Kuyambira nsonga ya kumpoto, ku mbali ya njira ya ku Hetiloni, polowera ku Hamati, Hazara-Enani ku malire a Damasiko kumpoto, ku mbali ya ku Hamati; ndi mbali zake zilinge kum’mawa ndi kumadzulo; Dani akhale nalo gawo limodzi.

2 Ndi m’malire a Dani, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Asere, limodzi.

3 Ndi m’malire a Asere, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Nafutali, limodzi.

4 Ndi m’malire a Nafutali, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Manase, limodzi.

5 Ndi m’malire a Manase, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Efuremu, limodzi.

6 Ndi m’malire a Efuremu, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Rubeni, limodzi.

7 Ndi m’malire a Rubeni, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Yuda, limodzi.

8 Ndi m’malire a Yuda, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo, pakhale chopereka muchipereke, mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu kupingasa kwake, ndi m’litali mwake lilingane ndi magawo enawo, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; ndi malo opatulika akhale pakati pake.

9 Chopereka muchipereke kwa Yehova chikhale cha mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu m’litali mwake, ndi zikwi khumi kupingasa kwake.

10 Ndipo m’mwemo mudzakhala chopereka chopatulika cha ansembe kumpoto, mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu m’litali mwake, ndi kumadzulo mikono zikwi khumi kupingasa kwake, ndi kum’mawa mikono zikwi khumi kupingasa kwake, ndi kumwera mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu m’litali mwake; ndi pakati pake pakhale malo opatulika a Yehova.

11 Chidzakhala cha ansembe opatulidwa a ana a Zadoki, amene anasunga udikiro wanga osasokera, muja anasokera ana a Israele, ndi muja anasokera Alevi.

12 Ndi chiperekocho chikhale chao chotapa pa chopereka cha dziko, ndicho chopatulika kwambiri pa malire a Alevi.

13 Ndipo polingana ndi malire a ansembe Alevi akhale nalo gawo la mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu m’litali mwake, ndi mikono zikwi khumi kupingasa kwake; m’litali mwake monse ndimo mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu, ndi kupingasa kwake mikono zikwi khumi.

14 Ndipo asagulitseko, kapena kulisintha, kapena kupitiriza zipatso zoyamba za dziko; pakuti lili lopatulika la Yehova.

15 Ndipo zikwi zisanu zotsalazo m’kupingasa kwake, chakuno cha mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu, zikhale za ntchito wamba za mzinda, za kumangapo zapabusa; ndi mzinda ukhale pakati pake.

16 Ndi miyeso yake ndi iyi: mbali ya kumpoto, mikono zikwi zinai mphambu mazana asanu; ndi mbali ya kumwera, mikono zikwi zinai mphambu mazana asanu; ndi mbali ya kum’mawa, mikono zikwi zinai mphambu mazana asanu; ndi mbali ya kumadzulo, mikono zikwi zinai mphambu mazana asanu.

17 Ndipo mzindawo ukhale ndi busa lake; kumpoto mikono mazana awiri mphambu makumi asanu, kumwera mikono mazana awiri mphambu makumi asanu, ndi kum’mawa mikono mazana awiri mphambu makumi asanu, ndi kumadzulo mikono mazana awiri mphambu makumi asanu.

18 Ndipo madera otsalawo m’litali mwake alingane ndi chopereka chopatulika, ndicho mikono zikwi khumi kum’mawa, ndi mikono zikwi khumi kamadzulo, alingane ndi chopereka chopatulika; ndi zipatso zake zikhale za chakudya cha iwo ogwira ntchito m’mzinda.

19 Iwo ogwira ntchito m’mzinda mwa mafuko onse a Israele alimeko.

20 Chopereka chonse ndicho mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu m’litali mwake, mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu kupingasa kwake; muchipereke chopereka chopatulika chaphwamphwa, pamodzi ndi dziko la mzindawo.

21 Ndipo madera ena otsalawo ndiwo a kalonga, mbali ina ndi ina ya chopereka chopatulika ndi ya dziko la mzinda, kutsogolo kwa mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu za chopereka kumalire a kum’mawa, ndi kumadzulo kutsogolo kwa mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu kumalire a kumadzulo, pandunji pa magawo enawo ndiwo cha kalonga; ndipo chopereka chopatulika ndi malo opatulika a Kachisi zidzakhala pakati pake.

22 Kuyambira tsono dziko la Alevi kufikira dziko la mzinda, ndiwo a pakati pa magawo ake a kalonga, pakati pa malire a Yuda ndi malire a Benjamini, kukhale kwa kalonga.

23 Kunena za mafuko otsala tsono, kuyambira kumbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo, Benjamini akhale nalo gawo limodzi.

24 Ndi kumalire a Benjamini, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Simeoni, gawo limodzi.

25 Ndi kumalire a Simeoni kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Isakara, limodzi.

26 Ndi kumalire a Isakara, kuyambira mbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Zebuloni, limodzi.

27 Ndi kumalire a Zebuloni, kuyambira kumbali ya kum’mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Gadi, limodzi.

28 Ndi ku malire a Gadi, mbali ya kumwera, kuloza kumwera, malire akhale kuyambira ku Tamara kufikira ku madzi a Meribati-Kadesi, ku mtsinje wa Ejipito, kufikira ku Nyanja Yaikulu.

29 Ili ndi dziko muligawire mafuko a Israele ndi kuchita maere, likhale cholowa chao; ndipo awa ndi magawo ao, ati Ambuye Yehova.

30 Ndipo malekezero a mzinda ndi awa: mbali ya kumpoto ayese mikono zikwi zinai mphambu mazana asanu;

31 ndi zipata za mzinda zidzakhala monga mwa maina a mafuko a Israele; zipata zitatu kumpoto: chipata chimodzi cha Rubeni, chipata chimodzi cha Yuda, chipata chimodzi cha Levi;

32 ndi ku mbali ya kum’mawa zikwi zinai mphambu mazana asanu, ndi zipata zitatu: chipata chimodzi cha Yosefe, chipata chimodzi cha Benjamini, chipata chimodzi cha Dani;

33 ndi kumbali ya kumwera ayese mikono zikwi zinai mphambu mazana asanu, ndi zipata zitatu: chipata chimodzi cha Simeoni, chipata chimodzi cha Isakara, chipata chimodzi cha Zebuloni;

34 kumbali ya kumadzulo mikono zikwi zinai mphambu mazana asanu, ndi zipata zake zitatu: chipata cha Gadi, chipata chimodzi cha Asere, chipata chimodzi cha Nafutali.

35 Pozungulira pake ndipo mikono zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu, ndi dzina la mzindawo kuyambira tsiku ilo lidzakhala, Yehova ali pomwepo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/48-8f0b9a7bb7686811b4fd4df6c6de6cb7.mp3?version_id=1068—

Categories
DANIELE

DANIELE Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli lidalembedwa pamene Ayuda ankazunzika kwambiri chifukwa cha malamulo ankhanza a mfumu yakunja. Wolemba bukuli alongosola zimene iye adaziwona m’masomphenya; afuna kuwalimbitsa mtima Ayudawo powauza kuti lidzabwera tsiku pamene Mulungu adzaithetsa mphamvu mfumu yoipa ija, mwakuti anthu ake adzapezanso ufulu.

Za m’masomphenyazi zikuwonetsa chiyambi chake ndiponso kutha kwake kwa maufumu angapo, kuyambira ufumu wa Babiloni; ndiponso zikulosa zakuti Mulungu adzawagwetsera pansi mafumu akunja aja ndi kupambanitsa anthu ake.

Bukuli lili ndi zigawo ziwiri: Gawo loyamba ndilo nkhani zokhudza Daniele ndi anzake ena okhala ku ukapolo ku Babiloni. Zikuwonetsa m’mene iwo anapambanira adani awo chifukwa chokhulupirira ndi kumvera Mulungu. Gawo lachiwiri likunena za m’masomphenya osiyanasiyana amene Daniele anawaona.

Za mkatimu

Daniele ndi abwenzi ake

1.1—6.28

Zina ndi zina zimene Daniele adaziwona m’masomphenya

7.1—11.45

a. Nyama zinai

7.1-28

b. Tonde ndi mbuzi

8.1—9.2

7

c. Wamthenga wakumwamba

10.1—11.45

d. Za nthawi yomaliza

12.1-13

Categories
DANIELE

DANIELE 1

Maleredwe a Daniele ndi anzake kwa mfumu ya ku Babiloni

1 Chaka chachitatu cha Yehoyakimu mfumu ya Yuda, Nebukadinezara mfumu ya ku Babiloni adadza kuYerusalemu, naumangira misasa ya nkhondo.

2 Ndipo Ambuye anapereka Yehoyakimu mfumu ya Yuda, m’dzanja lake, pamodzi ndi zipangizo zina za m’nyumba ya Mulungu, namuka nazo iye kudziko la Sinara, kunyumba ya mulungu wake, nalonga zipangizozo m’nyumba ya chuma cha mulungu wake.

3 Ndipo mfumu inauza Asipenazi mkulu wa adindo kuti abwere nao ena a ana a Israele, a mbeu ya mafumu, ndi ya akalonga;

4 anyamata opanda chilema, a maonekedwe okoma, a luso la nzeru zonse, ochenjera m’kudziwa, a luntha lakuganizira, okhoza kuimirira m’chinyumba cha mfumu; ndi kuti awaphunzitse m’mabuku, ndi manenedwe a Ababiloni.

5 Ndipo mfumu inawaikira gawo la chakudya cha mfumu tsiku ndi tsiku, ndi la vinyo wakumwa iye, ndi kuti awalere zaka zitatu, kuti potsiriza pake aimirire pamaso pa mfumu.

6 Mwa awa tsono munali a ana a Yuda, Daniele, Hananiya, Misaele, ndi Azariya.

7 Ndi mkulu wa adindo anawapatsa maina ena; Daniele anamutcha Belitesazara; ndi Hananiya, Sadrake; ndi Misaele, Mesaki; ndi Azariya, Abedenego.

8 Koma Daniele anatsimikiza mtima kuti asadzidetse ndi chakudya cha mfumu, kapena ndi vinyo amamwa; chifukwa chake anapempha mkulu wa adindo amlole asadzidetse.

9 Ndipo Mulungu anamkometsera Daniele mtima wa mkulu wa adindo, amchitire chifundo.

10 Nati mkulu wa adindo kwa Daniele, Ine ndiopa mbuyanga mfumu, amene anakuikirani chakudya chanu ndi chakumwa chanu; pakuti aonerenji nkhope zanu zachisoni zoposa za anyamata olingana ndi inu? Momwemo mudzapalamulitsa mutu wanga kwa mfumu.

11 Nati Daniele kwa kapitao, amene mkulu wa adindo adamuikayo ayang’anire Daniele, Hananiya, Misaele, ndi Azariya,

12 Muyesetu anyamata anu masiku khumi; atipatse zomera m’nthaka tidye, ndi madzi timwe.

13 Pamenepo mupenye maonekedwe athu ndi maonekedwe a anyamata akudya chakudya cha mfumu; ndi monga umo muonera, muchitire anyamata anu.

14 Ndipo anawamvera mau awa, nawayesa masiku khumi.

15 Atatha masiku khumiwo tsono, anaona kuti maonekedwe ao ndi kunenepa kwao anaposa anyamata onse adadyawo zakudya za mfumu.

16 Pamenepo kapitaoyo anachotsa chakudya chao ndi vinyo akadamwa, nawapatsa zomera m’nthaka.

17 Koma anyamata amene anai, Mulungu anawapatsa chidziwitso ndi luntha la m’mabuku ali onse, ndi nzeru; koma Daniele anali nalo luntha la m’masomphenya ndi maloto onse.

18 Atatha masiku inanenawo mfumu kuti alowe nao, mkulu wa adindo analowa nao pamaso pa Nebukadinezara.

19 Ndipo mfumu inalankhula nao, koma mwa iwo onse sanapezeke monga Daniele, Hananiya, Misaele, ndi Azariya; naimirira iwo pamaso pa mfumu.

20 Ndipo m’mau ali onse anzeru ndi aluntha, amene mfumu inawafunsira. Inawapeza akuposa alembi ndi openda onse mu ufumu wake wonse.

21 Nakhala moyo Daniele mpaka chaka choyamba cha mfumu Kirusi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DAN/1-79e11870cf0127030aa9dcab79300c50.mp3?version_id=1068—

Categories
DANIELE

DANIELE 2

Nebukadinezara alota, Daniele ammasulira lotolo

1 Chaka chachiwiri cha Nebukadinezara mfumu, Nebukadinezarayo analota maloto, ndi mzimu wake unavutika, ndi tulo take tidamwazikira.

2 Pamenepo mfumu inauza munthu aitane alembi, ndi openduza, ndi aula, ndi Ababiloni, amuululire mfumu maloto ake. Nalowa iwo, naimirira pamaso pa mfumu.

3 Niti nao mfumu, Ndalota loto, nuvutika mzimu wanga kudziwa lotolo.

4 Pamenepo Ababiloni anati kwa mfumu mu Chiaramu, Mfumu, mukhale ndi moyo chikhalire: mufotokozere anyamata anu lotoli, ndipo tidzakuuzani kumasulira kwake.

5 Niyankha mfumu, niti kwa Ababiloni, Chandichokera chinthuchi; mukapanda kundidziwitsa lotoli ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli, ndi nyumba zanu zidzayesedwa dzala.

6 Koma mukandidziwitsa lotoli, ndi kumasulira kwake, mudzalandira kwa ine mphatso, ndi mphotho, ndi ulemu waukulu; chifukwa chake mundidziwitse lotoli ndi kumasulira kwake.

7 Nabwerezanso iwo kuyankha, nati, Mfumu ifotokozere anyamata ake lotoli, ndipo tidzaidziwitsa kumasulira kwake.

8 Mfumu inayankha, niti, Ndidziwatu kuti mukunkhuniza dala, pakuona inu kuti chinthuchi chandichokera.

9 Koma mukapanda kundidziwitsa lotoli, mlandu wanu ndi umodzi; popeza mwapanganiranatu mau onama ndi oipa, kuwanena pamaso panga, mpaka idzasanduka nyengo; chifukwa chake mundifotokozere lotoli, momwemo ndidzadziwa kuti mudzandidziwitsa kumasulira kwake komwe.

10 Ababiloni anayankha pamaso pa mfumu, nati, Palibe munthu padziko lapansi wokhoza kuwulula mlandu wa mfumu; chifukwa chake palibe mfumu, mkulu, kapena wolamulira, wafunsira chinthu chotere kwa mlembi, kapena wopenduza, kapena Ababiloni ali onse.

11 Pakuti chinthu achifuna mfumu nchapatali; ndipo palibe wina wokhoza kuchiwulula pamaso pa mfumu, koma milungu imene kwao sikuli pamodzi ndi anthu.

12 Chifukwa chake mfumu inakwiya, nizaza kwambiri, nilamulira kuti awaphe anzeru onse mu Babiloni.

13 M’mwemo chilamulirocho chidamveka, ndi eni nzeru adati aphedwe; anafunafunanso Daniele ndi anzake aphedwe.

14 Pamenepo Daniele anabweza mau a uphungu wanzeru kwa Ariyoki mkulu wa olindirira a mfumu, adatulukawo kukapha eni nzeru a ku Babiloni;

15 anayankha nati kwa Ariyoki mkulu wa olindirira a mfumu, Chilamuliro cha mfumu chifulumiriranji? Pamenepo Ariyoki anadziwitsa Daniele chinthuchi.

16 Nalowa Daniele, nafunsa mfumu amuikire nthawi, kuti aululire mfumu kumasulira kwake.

17 Pamenepo Daniele anapita kunyumba kwake, nadziwitsa anzake Hananiya, Misaele, ndi Azariya, chinthuchi;

18 kuti apemphe zachifundo kwa Mulungu wa Kumwamba pa chinsinsi ichi; kuti Daniele ndi anzake asaonongeke pamodzi ndi eni nzeru ena a ku Babiloni.

19 Pamenepo chinsinsicho chinavumbulutsidwa kwa Daniele m’masomphenya a usiku. Ndipo Daniele analemekeza Mulungu wa Kumwamba.

20 Daniele anayankha, nati, Lilemekezedwe dzina la Mulungu kunthawi za nthawi, pakuti nzeru ndi mphamvu zili zake;

21 pakuti amasanduliza nthawi ndi nyengo, achotsa mafumu, nalonga mafumu, apatsa anzeru nzeru, ndi chidziwitso kwa iwo okhoza kuzindikira.

22 Iye avumbulutsa zinthu zakuya ndi zinsinsi; adziwa zokhala mumdima, ndi kuunika kumakhala kwa Iye.

23 Ndikuyamikani ndi kukulemekezani Inu, Mulungu wa makolo anga, pakuti mwandipatsa nzeru ndi mphamvu; ndipo mwandidziwitsa tsopano ichi tachifuna kwa Inu; pakuti mwatidziwitsa mlandu wa mfumu.

24 Potero Daniele analowa kwa Ariyoki amene mfumu idamuika aononge eni nzeru a ku Babiloni; anamuka, natero naye, Usaononga eni nzeru a ku Babiloni, undilowetse kwa mfumu, ndipo ndidzaululira mfumu kumasulirako.

25 Pamenepo Ariyoki analowa naye Daniele kwa mfumu mofulumira; natero nayo, Ndapeza munthu wa ana a ndende a Yuda, ndiye adzadziwitsa mfumu kumasulira kuja.

26 Mfumu inayankha, niti kwa Daniele, amene dzina lake ndiye Belitesazara, Ukhoza kodi kundidziwitsa lotolo ndidalilota, ndi kumasulira kwake?

27 Nayankha Daniele pamaso pa mfumu, nati, Chinsinsi inachitira liuma mfumu, angakhale anzeru, openduza, alembi, kapena alauli, sangathe kuchiululira mfumu;

28 koma kuli Mulungu Kumwamba wakuvumbulutsa zinsinsi; Iye ndiye wadziwitsa mfumu Nebukadinezara chimene chidzachitika masiku otsiriza. Loto lanu, ndi masomphenya a m’mtima mwanu pakama panu, ndi awa:

29 Inu mfumu, maganizo anu analowa m’mtima mwanu muli pakama panu, akunena za icho chidzachitika m’tsogolomo; ndipo Iye amene avumbulutsa zinsinsi wakudziwitsani chodzachitikacho.

30 Koma ine, chinsinsi ichi sichinavumbulutsidwe kwa ine chifukwa cha nzeru ndili nayo yakuposa wina aliyense wamoyo, koma kuti kumasuliraku kudziwike kwa mfumu, ndi kuti mudziwe maganizo a mtima wanu.

31 Inu mfumu munapenya ndi kuona fano lalikulu. Fanoli linali lalikulu, ndi kunyezimira kwake kunaposa; linali kuima popenyana ndi inu, ndi maonekedwe ake anali oopsa.

32 Fano ili tsono, mutu wake unali wagolide wabwino, chifuwa chake ndi manja ake zasiliva, mimba yake ndi chuuno chake zamkuwa,

33 miyendo yake yachitsulo, mapazi ake mwina chitsulo mwina dongo.

34 Munali chipenyere kufikira mwala unasemedwa popanda manja, umene unagunda fanoli pa mapazi ake okhala chitsulo ndi dongo, nuwaphwanya.

35 Pamenepo chitsulo, dongo, mkuwa, siliva, ndi golide, zinapereka pamodzi, ndipo zinasanduka ngati mungu wa pa madwale a malimwe; ndi mphepo inaziuluza, osapezekanso malo ao; ndi mwala udagunda fanowo unasanduka phiri lalikulu, nudzaza dziko lonse lapansi.

36 Ili ndi loto; kumasulira kwake tsono tikufotokozerani mfumu.

37 Inu mfumu ndinu mfumu ya mafumu, pakuti Mulungu wa Kumwamba anakupatsani ufumu, ndi mphamvu yaikulu, ndi ulemu;

38 ndipo paliponse pokhala ana a anthu Iye anapereka nyama zakuthengo, ndi mbalame za m’mlengalenga, m’dzanja lanu; nakuchititsani ufumu pa izi zonse; inu ndinu mutuwo wagolide.

39 Ndi pambuyo pa inu padzauka ufumu wina wochepa ndi wanu, ndi ufumu wina wachitatu wamkuwa wakuchita ufumu padziko lonse lapansi.

40 Ndi ufumu wachinai udzakhala wolimba ngati chitsulo, popeza chitsulo chiphwanya ndi kufoketsa zonse; ndipo monga chitsulo chiswa zonsezi, uwu udzaphwanya ndi kuswa.

41 Ndipo umo mudaonera mapazi ndi zala zake, mwina dongo la woumba, mwina chitsulo; ufumuwo udzakhala wogawanika, koma momwemo mudzakhala mphamvu ya chitsulo; popeza mudaona chitsulo chosakanizika ndi dongo.

42 Ndi zala za mapazi, mwina chitsulo ndi mwina dongo, momwemo ufumuwo, mwina wolimba mwina wogamphuka.

43 Ndi umo mudaonera chitsulo chosakanizika ndi dongo, iwo adzadzisokoneza ndi ana a anthu wamba; koma sadzaphatikizana, monga umo chitsulo sichimasakanizikana ndi dongo.

44 Ndipo masiku a mafumu aja Mulungu wa Kumwamba adzaika ufumu woti sudzaonongeka kunthawi zonse, ndi ulamuliro wake sudzasiyidwira mtundu wina wa anthu, koma udzaphwanya ndi kutha maufumu ao onse, nudzakhala chikhalire.

45 Umo mudaonera kuti mwala unasemedwa m’phiri popanda manja, ndi kuti udapera chitsulo, mkuwa, dongo, siliva, ndi golide; Mulungu wamkulu wadziwitsa mfumu chidzachitika m’tsogolomo; lotoli nloona, ndi kumasulira kwake kwakhazikika.

46 Pamenepo mfumu Nebukadinezara anagwa nkhope yake pansi, nalambira Daniele, nati amthirire nsembe yaufa ndi ya zonunkhira zokoma.

47 Mfumu inamyankha Daniele, niti, Zoona Mulungu wako ndiye Mulungu wa milungu, ndi Mbuye wa mafumu, ndi wovumbulutsa zinsinsi; popeza wakhoza kuvumbulutsa chinsinsi ichi.

48 Pamenepo mfumu inasandutsa Daniele wamkulu, nimpatsa mphatso zazikulu zambiri, namlamuliritsa dera lonse la ku Babiloni; nakhala iye kazembe wamkulu wa anzeru onse a ku Babiloni.

49 Pamenepo Daniele anapempha mfumu, ndipo anaika Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, ayang’anire ntchito za dera la ku Babiloni. Koma Daniele anakhala m’bwalo la mfumu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DAN/2-903d3415070c68b9b78d917b294b1e90.mp3?version_id=1068—

Categories
DANIELE

DANIELE 3

Nebukadinezara apanga fano lagolide

1 Mfumu Nebukadinezara anapanga fano lagolide, msinkhu wake mikono makumi asanu ndi limodzi, ndi thunthu lake mikono isanu ndi umodzi; analiimika pa chidikha cha Dura, m’dera la ku Babiloni.

2 Ndipo mfumu Nebukadinezara inatumiza kukasonkhanitsa akalonga, akazembe, ndi ziwanga, oweruza, akulu osunga chuma, mandoda, ankhoswe, ndi olamulira onse a madera, abwere kuzulula fanoli adaliimika mfumu Nebukadinezara.

3 Pamenepo akalonga, akazembe, ndi ziwanga, oweruza, akulu osunga chuma, mandoda, ankhoswe, ndi olamulira onse a madera, anasonkhanira kupereka fano adaliimika mfumu Nebukadinezara, naimirira pamaso pa fano adaliimika Nebukadinezara.

4 Ndipo wolalikira anafuulitsa, kuti, Akulamulirani inu anthu, mitundu ya anthu a manenedwe osiyana,

5 kuti pakumva inu mau a lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, ngoli, ndi zoimbitsa zilizonse, mugwadire ndi kulambira fano lagolide adaliimika mfumu Nebukadinezara;

6 ndipo aliyense wosagwadira ndi kulambira, adzaponyedwa nthawi yomweyo m’kati mwa ng’anjo yotentha yamoto.

7 Potero nthawi yomweyo pakumva anthu onse mau a lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, ndi zoimbitsa zilizonse, anthu onse, mitundu ya anthu a manenedwe osiyana, anagwadira, nalambira fano lagolide adaliimika mfumu Nebukadinezara.

8 Chifukwa chake anayandikira Ababiloni ena nthawi yomweyi, naneneza Ayuda.

9 Anayankha, nati kwa mfumu Nebukadinezara, Mfumu, mukhale ndi moyo chikhalire.

10 Inu mfumu mwalamulira kuti munthu aliyense amene adzamva mau a lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, ngoli, ndi zoimbitsa zilizonse, agwadire, nalambire fanolo lagolide;

11 ndi yense wosagwadira ndi kulambira adzaponyedwa m’kati mwa ng’anjo yotentha yamoto.

12 Alipo Ayuda amene munawaika ayang’anire ntchito ya dera la ku Babiloni, Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, amuna awa, mfumu, sanasamalire inu, satumikira milungu yanu, kapena kulambira fano lagolide mudaliimikalo.

Anzake a Daniele aponyedwa m’ng’anjo yamoto

13 Pamenepo Nebukadinezara, mumkwiyo ndi mu ukali wake, anawauza abwere nao Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego. Ndipo anabwera nao amunawa kwa mfumu.

14 Nebukadinezara anayankha, nati kwa iwo, Kodi mutero dala, Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, kusatumikira milungu yanga, ndi kusalambira fano lagolide ndinaliimikalo?

15 Mukavomereza tsono, pakumva mau a lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, ndi ngoli, ndi zoimbitsa zilizonse, kugwadira ndi kulambira fano ndinalipanga, chabwino; koma mukapanda kulambira, mudzaponyedwa nthawi yomweyi m’kati mwa ng’anjo yotentha yamoto; ndipo mulungu yemwe adzakulanditsani m’manja mwanga ndani?

16 Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, anayankha, nati kwa mfumu Nebukadinezara, Sikufunika kuti tikuyankheni pa mlandu uwu.

17 Taonani, Mulungu wathu amene timtumikira akhoza kutilanditsa m’ng’anjo yotentha yamoto, nadzatilanditsa m’dzanja lanu, mfumu.

18 Koma akapanda kutero, dziwani, mfumu, kuti sitidzatumikira milungu yanu, kapena kulambira fano lagolide mudaliimikalo.

19 Pamenepo Nebukadinezara anadzazidwa ndi ukali, ndi maonekedwe a nkhope yake anasandulikira Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego; anayankha, nati asonkheze ng’anjo kasanu ndi kawiri koposa umo amasonkhezera.

20 Nauza amuna ena amphamvu a m’khamu lake la nkhondo amange Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, ndi kuwaponya m’ng’anjo yotentha yamoto.

21 Pamenepo amuna awa anamangidwa ali chivalire zofunda zao, malaya ao, ndi nduwira zao, ndi zovala zao zina; naponyedwa m’kati mwa ng’anjo yotentha yamoto.

22 Motero, popeza mau a mfumu anafulumiza, ndi ng’anjo inatentha koposa, lawi la moto linapha iwo aja ananyamula Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego.

23 Ndipo amuna atatu awa, Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, anagwa pansi omangidwa m’kati mwa ng’anjo yotentha yamoto.

24 Pamenepo mfumu Nebukadinezara anadabwa, nauka msanga, nanena nati kwa mandoda ake, Kodi sitinaponye amuna atatu omangidwa m’kati mwa moto? Anayankha nati kwa mfumu, Inde mfumu.

25 Anayankha, nati, Taonani, ndilikuona amuna anai omasuka, alikuyenda m’kati mwa moto; ndipo alibe kuphwetekwa, ndi maonekedwe a wachinai akunga mwana wa milungu.

26 Pamenepo Nebukadinezara anayandikira pa khomo la ng’anjo yotentha yamoto, analankhula, nati, Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, inu atumiki a Mulungu Wam’mwambamwamba, tulukani, idzani kuno. Pamenepo Sadrake, Mesake, ndi Abedenego, anatuluka m’kati mwa moto.

27 Ndipo akalonga, akazembe, ndi ziwanga, ndi mandoda a mfumu, atasonkhana, anaona amuna awa, kuti moto unalibe mphamvu pa matupi ao, losawauka tsitsi la pamutu pao, ndi zofunda zao zosasandulika, fungo lomwe lamoto losawaomba.

28 Nebukadinezara ananena, nati, Alemekezedwe Mulungu wa Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, amene anatuma mthenga wake, napulumutsa atumiki ake omkhulupirira Iye, nasanduliza mau a ine mfumu, napereka matupi ao kuti asatumikire kapena kulambira mulungu wina yense, koma Mulungu waowao.

29 Chifukwa chake ndilamulira kuti anthu ali onse, mtundu uliwonse, ndi a manenedwe ali onse, akunenera molakwira Mulungu wa Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, adzadulidwa nthulinthuli, ndi nyumba zao zidzasanduka dzala; popeza palibe mulungu wina akhoza kulanditsa motero.

30 Pamenepo mfumu inakuza Sadrake, Mesaki, ndi Abedenego, m’dera la ku Babiloni.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DAN/3-36d3dcc9ef3cc11b8ec5ddbe136c7672.mp3?version_id=1068—