Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 3

Malangizo a kuopa, kukhulupirira, ndi kumvera Yehova

1 Mwananga, usaiwale malamulo anga,

mtima wako usunge malangizo anga;

2 pakuti adzakuonjezera masiku ambiri,

ndi zaka za moyo ndi mtendere.

3 Chifundo ndi choonadi zisakusiye;

uzimange pakhosi pako;

uzilembe pamtima pako;

4 motero udzapeza chisomo ndi nzeru yabwino,

pamaso pa Mulungu ndi anthu.

5 Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,

osachirikizika pa luntha lako;

6 umlemekeze m’njira zako zonse,

ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

7 Usadziyese wekha wanzeru;

opa Yehova, nupatuke pazoipa;

8 mitsempha yako idzalandirapo moyo,

ndi mafupa ako uwisi.

9 Lemekeza Yehova ndi chuma chako,

ndi zinthu zako zonse zoyambirira kucha;

10 motero nkhokwe zako zidzangoti thee,

mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11 Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,

ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwake;

12 pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;

monga atate mwana amene akondwera naye.

Phindu la Nzeru

13 Wodala ndi wopeza nzeru,

ndi woona luntha;

14 pakuti malonda a nzeru aposa malonda asiliva,

phindu lake liposa golide woyengeka.

15 Mtengo wake uposa ngale;

ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

16 Masiku ambiri ali m’dzanja lamanja lake;

chuma ndi ulemu m’dzanja lake lamanzere.

17 Njira zake zili zokondweretsa,

mayendedwe ake onse ndiwo mtendere.

18 Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;

wakuiumirira ngwodala.

19 Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;

naika zamwamba ndi luntha.

20 Zakuya zinang’ambika ndi kudziwa kwake;

thambo ligwetsa mame.

21 Mwananga, zisachokere kumaso ako;

sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

22 ndipo mtima wako udzatengapo moyo,

ndi khosi lako chisomo.

23 Pompo udzayenda m’njira yako osaopa,

osaphunthwa phazi lako.

24 Ukagona, sudzachita mantha;

udzagona tulo tokondweretsa.

25 Usaope zoopsa zodzidzimutsa,

ngakhale zikadza zopasula oipa;

26 pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,

nadzasunga phazi lako lingakodwe.

Malangizo ena osiyana

27 Oyenera kulandira zabwino usawamane;

pokhoza dzanja lako kuwachitira zabwino.

28 Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,

ndipo mawa ndidzakupatsa;

pokhala uli nako kanthu.

29 Usapangire mnzako chiwembu;

popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.

30 Usakangane ndi munthu chabe,

ngati sanakuchitire choipa.

31 Usachitire nsanje munthu wachiwawa;

usasankhe njira yake iliyonse.

32 Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;

koma chinsinsi chake chili ndi oongoka.

33 Yehova atemberera za m’nyumba ya woipa;

koma adalitsa mokhalamo olungama.

34 Anyozadi akunyoza,

koma apatsa akufatsa chisomo.

35 Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao;

koma opusa adzakweza manyazi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/3-e517f48ff8327cd8228c94a3e6c5b797.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 4

Chenjezo lakuti afune Nzeru nalewe njira za oipa

1 Ananu, mverani mwambo wa atate,

nimutchere makutu mukadziwe luntha;

2 pakuti ndikuphunzitsani zabwino;

musasiye chilangizo changa.

3 Pakuti ndinali mwana kwa atate wanga,

wokondedwa ndi mai, ndine ndekha, sanabale wina.

4 Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine,

mtima wako uumirire mau anga;

sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.

5 Tenga nzeru, tenga luntha;

usaiwale, usapatuke pa mau a m’kamwa mwanga;

6 usasiye nzeru, ndipo idzakusunga;

uikonde, idzakutchinjiriza.

7 Nzeru ipambana, tatenga nzeru;

m’kutenga kwako konseko utenge luntha.

8 Uilemekeze, ndipo idzakukweza;

idzakutengera ulemu pamene uifungatira.

9 Idzaika chisada cha chisomo pamutu pako;

idzakupatsa korona wokongola.

10 Tamvera mwananga, nulandire mau anga;

ndipo zaka za moyo wako zidzachuluka.

11 Ndakuphunzitsa m’njira ya nzeru,

ndakuyendetsa m’mayendedwe olungama.

12 Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;

ukathamanga, sudzaphunthwa.

13 Gwira mwambo, osauleka;

uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

14 Usalowe m’mayendedwe ochimwa,

usayende m’njira ya oipa.

15 Pewapo, osapitamo;

patukapo, nupitirire.

16 Pakuti akapanda kuchita zoipa, samagona;

ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwachokera.

17 Pakuti amadya chakudya cha uchimo,

namwa vinyo wa chifwamba.

18 Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbandakucha,

kunkabe kuwala kufikira usana woti mbee.

19 Njira ya oipa ikunga mdima;

sadziwa chimene chiwaphunthwitsa.

20 Mwananga, tamvera mau anga;

tcherera makutu ku zonena zanga.

21 Asachoke kumaso ako;

uwasunge m’kati mwa mtima wako.

22 Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza,

nalamitsa thupi lao lonse.

23 Chinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga;

pakuti magwero a moyo atulukamo.

24 Tasiya m’kamwa mokhota,

uike patali milomo yopotoka.

25 Maso ako ayang’ane m’tsogolo,

zikope zako zipenye moongoka.

26 Sinkhasinkha bwino mayendedwe a mapazi ako;

njira zako zonse zikonzeke.

27 Usapatuke kudzanja lamanja kapena kulamanzere;

suntha phazi lako kusiya zoipa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/4-4bebf0641029010d0e0755c15bc99f54.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 5

Achenjere naye mkazi woipa

1 Mwananga, mvera nzeru yanga;

tcherera makutu ku luntha langa;

2 ukasunge zolingalira,

milomo yako ilabadire zomwe udziwa.

3 Pakuti milomo ya mkazi wachiwerewere ikukha uchi;

m’kamwa mwake muti see koposa mafuta.

4 Chimaliziro chake nchowawa ngati chivumulo,

ndi chakuthwa ngati lupanga lakuthawa konsekonse.

5 Mayendedwe ake atsikira kuimfa;

mapazi ake aumirira kumanda;

6 sasinkhasinkha bwino za njira ya moyo;

mayendedwe ake adzandira dzandidzandi osadziwa iye.

7 Ndipo tsopano ana, mundimvere,

musapatuke ku mau a m’kamwa mwanga.

8 Siyanitsa njira yako kutali kwa iyeyo,

osayandikira ku khomo la nyumba yake;

9 kuti ungapereke ulemu wako kwa ena,

ndi zaka zako kwa ankhanza;

10 kuti mphamvu yako isakhutitse alendo,

ndi kuti usagwire ntchito m’nyumba ya wachilendo;

11 ungalire pa chimaliziro chako,

pothera nyama yako ndi thupi lako;

12 ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo,

mtima wanga ndi kunyoza chidzudzulo;

13 ndipo sindinamvere mau a aphunzitsi anga;

ngakhale kutcherera makutu kwa akundilanga mwambo!

14 Ndikadakhala m’zoipa zonse,

m’kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.

15 Imwa madzi a m’chitsime mwako,

ndi madzi oyenda a m’kasupe mwako.

16 Kodi magwero ako ayenera kumwazika kunja,

ndi mitsinje ya madzi m’makwalala?

17 Ikhale ya iwe wekha,

si ya alendo okhala nawe ai.

18 Adalitsike kasupe wako;

ukondwere ndi mkazi wokula nayo.

19 Ngati mbawala yokonda ndi chinkhoma chachisomo,

maere ake akukwanire nthawi zonse;

ukodwe ndi chikondi chake osaleka.

20 Pakuti ukondwerenji, mwananga, ndi mkazi wachiwerewere,

ndi kufungatira chifuwa cha mkazi wachilendo?

21 Pakuti njira za munthu zili pamaso pa Yehova,

asinkhasinkha za mayendedwe ake onse.

22 Zoipa zakezake zidzagwira woipa;

adzamangidwa ndi zingwe za uchimo wake.

23 Adzafa posowa mwambo;

adzasochera popusa kwambiri.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/5-bbbe90f0618659e9199c566ac200b145.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 6

Za kuperekera mnzake chikole

Zisanu ndi ziwiri zoipira Mulungu

1 Mwananga, ngati waperekera mnzako chikole,

ngati wapangana kulipirira mlendo,

2 wakodwa ndi mau a m’kamwa mwako,

wagwidwa ndi mau a m’kamwa mwako.

3 Chita ichi tsono; mwananga, nudzipulumutse;

popeza walowa m’dzanja la mnzako,

pita nudzichepetse, numdandaulire mnzako.

4 Usaone tulo m’maso mwako,

ngakhale kuodzera zikope zako.

5 Dzipulumutse wekha ngati mphoyo kudzanja la msaki,

ndi mbalame kudzanja la msodzi.

6 Pita kunyerere, waulesi iwe,

penya njira zao nuchenjere;

7 zilibe mfumu,

ngakhale kapitao, ngakhale mkulu;

8 koma zitengeratu zakudya zao m’malimwe;

ndipo zituta dzinthu zao m’masika.

9 Udzagona mpaka liti, waulesi iwe?

Udzauka kutulo tako liti?

10 Tulo tapang’ono, kuodzera pang’ono,

kungomanga manja pang’ono, ndi kugona;

11 ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala,

ndi kusauka kwako ngati munthu wachikopa.

12 Munthu wopanda pake, mwamuna wamphulupulu;

amayenda ndi m’kamwa mokhota.

13 Amatsinzinira ndi maso ake, napalasira ndi mapazi ake,

amalankhula ndi zala zake;

14 zopotoka zili m’mtima mwake, amaganizira zoipa osaleka;

amapikisanitsa anthu.

15 Chifukwa chake tsoka lake lidzadza modzidzimuka;

adzasweka msangamsanga, palibe chompulumutsa.

16 Zilipo zinthu zisanu ndi chimodzi Yehova azida;

ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa:

17 Maso akunyada, lilime lonama,

ndi manja akupha anthu osachimwa;

18 mtima woganizira ziwembu zoipa,

mapazi akuthamangira mphulupulu m’mangum’mangu;

19 mboni yonama yonong’ona mabodza,

ndi wopikisanitsa abale.

20 Mwananga, sunga malangizo a atate wako,

usasiye malamulo a mai ako;

21 uwamange pamtima pako osaleka;

uwalunze pakhosi pako.

22 Adzakutsogolera ulikuyenda,

ndi kukudikira uli m’tulo,

ndi kulankhula nawe utauka.

23 Pakuti malangizo ndi nyali, malamulo ndi kuunika;

ndi zidzudzulo za mwambo ndizo njira ya moyo.

24 Zikutchinjiriza kwa mkazi woipa,

ndi kulilime losyasyalika la mkazi wachiwerewere.

25 Asakuchititse kaso m’mtima mwako,

asakukole ndi zikope zake.

26 Pakuti ukayamba ndi mkazi wadama,

udzamaliza ndi nyenyeswa;

ndipo mkazi wa mwini amasaka moyo wa mtengowapatali.

27 Kodi mwamuna angatenge moto pa chifuwa chake,

osatentha zovala zake?

28 Pena kodi mwamuna angayende pa makala oyaka,

osapsa mapazi ake?

29 Chomwecho wolowa kwa mkazi wa mnzake;

womkhudzayo sadzapulumuka chilango.

30 Anthu sanyoza mbala ikaba,

kuti ikhutitse mtima wake pomva njala;

31 koma ikapezedwa idzabwezera kasanu ndi kawiri;

idzapereka chuma chonse cha m’nyumba yake.

32 Wochita chigololo ndi mkazi alibe nzeru;

wofuna kuononga moyo wakewake ndiye amatero.

33 Adzalasidwa nanyozedwa;

chitonzo chake sichidzafafanizidwe.

34 Pakuti nsanje ndiyo ukali wa mwamuna,

ndipo sadzachitira chifundo tsiku lobwezera chilango.

35 Sadzalabadira chiombolo chilichonse,

sadzapembedzeka ngakhale uchulukitsa malipo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/6-002dadb40a0570935a603f53806bf402.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 7

Achenjere naye mkazi woipa

1 Mwananga, sunga mau anga,

ukundike malangizo anga,

2 Sunga malangizo anga, nukhale ndi moyo;

ndi malamulo anga ngati mwana wa diso lako.

3 Uwamange pa zala zako,

uwalembe pamtima pako.

4 Nena kwa nzeru, Ndiwe mlongo wanga;

nutche luntha mbale wako.

5 Kuti zikutchinjirizire kwa mkazi wachiwerewere,

kwa mlendo wamkazi wosyasyalika ndi mau ake.

6 Pakuti pa zenera la nyumba yanga

ndinapenyera pamwamba pake;

ndinaona pakati pa achibwana,

7 ndinazindikira pakati pa aang’ono

mnyamata wopanda nzeru,

8 alikupita pakhwalala pafupi ndi mphambano ya pa mkaziyo,

ndi kuyenda panjira ya kunyumba yake;

9 pa madzulo kuli sisiro,

pakati pa usiku pali mdima.

10 Ndipo taona, mkaziyo anamchingamira,

atavala zadama wochenjera mtima,

11 ali wolongolola ndi wosaweruzika,

mapazi ake samakhala m’nyumba mwake.

12 Mwina ali kumakwalala, mwina ali kumabwalo,

nabisalira pa mphambano zonse.

13 Ndipo anagwira mnyamatayo, nampsompsona;

nati kwa iye ndi nkhope yachipongwe,

14 nsembe zamtendere zili nane;

lero ndachita zowinda zanga.

15 Chifukwa chake ndatuluka kudzakuchingamira,

kudzafunitsa nkhope yako, ndipo ndakupeza.

16 Ndayala zofunda pakama panga,

nsalu zamawangamawanga za thonje la ku Ejipito,

17 ndakapiza pamphasa panga mankhwala onunkhira amure

ndi chisiyo ndi sinamoni.

18 Tiye tikondwere ndi chikondano mpaka mamawa;

tidzisangalatse ndi chiyanjano.

19 Pakuti mwamuna kulibe kwathu,

wapita ulendo wa kutali;

20 watenga thumba la ndalama m’dzanja lake,

tsiku lowala mwezi adzabwera kwathu.

21 Amkakamiza ndi kukoka kwa mau ake,

ampatutsa ndi kusyasyalika kwa milomo yake.

22 Mnyamatayo amtsata posachedwa,

monga ng’ombe ipita kukaphedwa;

ndi monga unyolo umadza kulanga chitsiru;

23 mpaka muvi ukapyoza mphafa yake;

amtsata monga mbalame yothamangira msampha;

osadziwa kuti adzaononga moyo wake.

24 Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine,

labadirani mau a m’kamwa mwanga.

25 Mtima wako usapatukire kunjira ya mkaziyo,

usasochere m’mayendedwe ake.

26 Pakuti amagwetsa ambiri, atawalasa;

ndipo ophedwa ndi iye achulukadi.

27 Nyumba yake ndiyo njira ya kumanda,

yotsikira kuzipinda za imfa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/7-27422fd7823f7b616ef37a976cfa2d76.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 8

Nzeru ipambana m’kuchita kwake

1 Kodi nzeru siitana,

luntha ndi kukweza mau ake?

2 Iima pamwamba pa mtunda,

pa mphambano za makwalala;

3 pambali pa chipata polowera m’mudzi,

polowa anthu pa makomo ifuula:

4 Ndinu ndikuitanani, amuna,

mau anga ndilankhula kwa ana a anthu.

5 Achibwana inu, chenjerani,

opusa inu, khalani ndi mtima wozindikira;

6 imvani, pakuti ndikanena zoposa,

ndi zolungama potsegula pakamwa panga.

7 Pakuti m’kamwa mwanga mudzalankhula ntheradi,

zoipa zinyansa milomo yanga.

8 Mau onse a m’kamwa mwanga alungama;

mwa iwo mulibe zokhota ndi zopotoka.

9 Onsewo amveka ndi iye amene azindikira;

alungama kwa akupeza nzeru.

10 Landirani mwambo wanga, sisilivaai;

ndi nzeru kopambana ndi golide wosankhika.

11 Pakuti nzeru iposa ngale,

ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo.

12 Ine Nzeru ndikhala m’kuchenjera, ngati m’nyumba yanga;

ndimapeza kudziwa ndi zolingalira.

13 Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa;

kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa,

ndi m’kamwa mokhota, ndizida.

14 Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa;

ndine luntha; ndili ndi mphamvu.

15 Mwa ine mafumu alamulira;

akazembe naweruza molungama.

16 Mwa ine akalonga ayang’anira,

ndi akulu, ngakhale oweruza onse a m’dziko.

17 Akundikonda ndiwakonda;

akundifunafuna adzandipeza.

18 Katundu ndi ulemu zili ndi ine,

chuma chosatha ndi chilungamo.

19 Chipatso changa chiposa golide, ngakhale golide woyengeka;

phindu langa liposa siliva wosankhika.

20 Ndimayenda m’njira ya chilungamo,

pakati pa mayendedwe a chiweruzo,

21 kuti ndionetse chuma akundikonda, chikhale cholowa chao,

ndi kudzaza mosungira mwao.

Nzeru ndiyo ya nthawi yosayamba

22 Yehova anali nane poyamba njira yake,

asanalenge zake zakale.

23 Anandiimika chikhalire chiyambire,

dziko lisanalengedwe.

24 Pamene panalibe zozama ndinabadwa ine,

pamene panalibe akasupe odzala madzi.

25 Mapiri asanakhazikike,

zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa.

26 Asanalenge dziko, ndi thengo,

ngakhale chiyambi cha fumbi la dziko.

27 Pamene anakhazika mlengalenga ndinali pompo;

pamene analemba pazozama kwetekwete;

28 polimbitsa Iye thambo la kumwamba,

pokula akasupe a zozama.

29 Poikira nyanja malire ake,

kuti madzi asapitirire pa lamulo lake;

polemba maziko a dziko.

30 Ndinali pa mbali pake ngati mmisiri;

ndinamsekeretsa tsiku ndi tsiku,

ndi kukondwera pamaso pake nthawi zonse;

31 ndi kukondwera ndi dziko lake lokhalamo anthu,

ndi kusekerera ndi ana a anthu.

32 Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine,

ngodala akusunga njira zanga.

33 Imvani mwambo, mukhale anzeru osaukana.

34 Ngwodala amene andimvera,

nadikira pa zitseko zanga tsiku ndi tsiku,

ndi kulinda pa mphuthu za makoma anga;

35 pakuti wondipeza ine apeza moyo;

Yehova adzamkomera mtima.

36 Koma wondichimwira apweteka moyo wake;

onse akundida ine akonda imfa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/8-65b70aedaa5e09db561e00a6b605e874.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 9

Madyerero a Nzeru

1 Nzeru yamanga nyumba yake,

yasema zoimiritsa zake zisanu ndi ziwiri;

2 yaphera nyama yake, nisakaniza vinyo wake,

nilongosolanso pa gome lake.

3 Yatuma anamwali ake, iitana

pa misanje ya m’mudzi.

4 Wazibwana yense apatukire kuno;

iti kwa yense wosowa nzeru,

5 Tiyeni, idyani chakudya changa;

nimumwe vinyo wanga ndamsakaniza.

6 Lekani, achibwana inu, nimukhale ndi moyo;

nimuyende m’njira ya nzeru.

7 Woweruza munthu wonyoza adzichititsa yekha manyazi;

yemwe adzudzula wochimwa angodetsa mbiri yakeyake.

8 Usadzudzule wonyoza kuti angakude;

dzudzula wanzeru adzakukonda.

9 Ukachenjeza wanzeru adzakulitsa nzeru yake;

ukaphunzitsa wolungama adzaonjezera kuphunzira.

10 Chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova;

kudziwa Woyerayo ndiko luntha.

11 Pakuti mwa ine masiku ako adzachuluka,

zaka za moyo wako zidzaonjezedwa.

12 Ukakhala wanzeru, si yakoyako nzeruyo?

Ndipo ukanyoza udzasauka wekha.

13 Utsiru umalongolola,

ngwa chibwana osadziwa kanthu.

14 Ukhala pa khomo la nyumba yake,

pampando pa misanje ya m’mudzi,

15 kuti uitane akupita panjira,

amene angonkabe m’kuyenda kwao,

16 wachibwana ndani? Apatukire kuno.

Ati kwa yense wopanda nzeru,

17 madzi akuba atsekemera,

ndi chakudya chobisika chikoma.

18 Ndipo mwamunayo sadziwa kuti akufa ali konko;

omwe achezetsa utsiru ali m’manda akuya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/9-f14cb55a6d54b6ebae11a55edb662d4b.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 10

Miyambo yosiyanasiyana

Miyambo ya Solomoni:

1 Mwana wanzeru akondweretsa atate;

koma mwana wopusa amvetsa amake chisoni.

2 Chuma cha uchimo sichithangata;

koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.

3 Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;

koma amainga chifuniro cha wochimwa.

4 Wochita ndi dzanja laulesi amasauka;

koma dzanja la akhama lilemeretsa.

5 Wokolola m’malimwe ndi mwana wanzeru;

koma wogona pakututa ndi mwana wochititsa manyazi.

6 Madalitso ali pamutu pa wolungama;

koma m’kamwa mwa oipa mubisa chiwawa.

7 Amayesa wolungama wodala pomkumbukira;

koma dzina la oipa lidzavunda.

8 Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;

koma chitsiru cholongolola chidzagwa.

9 Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;

koma wokhotetsa njira zake adzadziwika.

10 Wotsinzinira achititsa chisoni;

koma wodzudzula momveka achita mtendere.

11 M’kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;

koma m’kamwa mwa oipa mubisa chiwawa.

12 Udani upikisanitsa;

koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

13 Nzeru ipezedwa m’milomo ya wozindikira;

koma wopusa pamsana pake nthyole.

14 Anzeru akundika zomwe adziwa;

koma m’kamwa mwa chitsiru muononga tsopano lino.

15 Chuma cha wolemera ndi mzinda wake wolimba;

koma umphawi wao uononga osauka.

16 Ntchito za wolungama zipatsa moyo;

koma phindu la oipa lichimwitsa.

17 Wosunga mwambo ali m’njira ya moyo;

koma wosiya chidzudzulo asochera.

18 Wobisa udani ali ndi milomo yonama;

wonena ugogodi ndiye chitsiru.

19 Pochuluka mau zolakwa sizisoweka;

koma wokhala chete achita mwanzeru.

20 Lilime la wolungama likungasilivawosankhika;

koma mtima wa oipa uli wachabe.

21 Milomo ya wolungama imadyetsa ambiri;

koma zitsiru zimafa posowa nzeru.

22 Madalitso a Yehova alemeretsa,

saonjezerapo chisoni.

23 Masewero a chitsiru ndiwo kuchita zoipa;

koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

24 Chomwe woipa achiopa chidzamfikira;

koma chomwe olungama achifuna chidzapatsidwa.

25 Monga kavumvulu angopita, momwemo woipa kuli zii;

koma olungama ndiwo maziko osatha.

26 Ngati vinyo wowawa m’mano, ndi utsi m’maso,

momwemo waulesi kwa iwo amene amtuma.

27 Kuopa Yehova kutanimphitsa masiku;

koma zaka za oipa zidzafinimpha.

28 Chiyembekezo cha olungama ndicho chimwemwe;

koma chidikiro cha oipa chidzaonongeka.

29 Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima;

koma akuchita zoipa adzaonongeka.

30 Wolungama sadzachotsedwa konse;

koma oipa sadzakhalabe m’dziko.

31 M’kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru;

koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32 Milomo ya wolungama idziwa zokondweretsa;

koma m’kamwa mwa oipa munena zokhota.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/10-6640647a67135114988aab0e34b398f7.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 11

1 Muyeso wonyenga unyansa Yehova;

koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

2 Pakudza kudzikuza padzanso manyazi;

koma nzeru ili ndi odzichepetsa.

3 Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera;

koma kukhota kwa achiwembu kudzawaononga.

4 Chuma sichithandiza tsiku la mkwiyo;

koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.

5 Chilungamo cha wangwiro chimaongola njira yake;

koma woipa adzagwa ndi zoipa zake.

6 Chilungamo cha oongoka mtima chidzawapulumutsa;

koma achiwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.

7 Pomwalira woipa chidikiro chake chionongeka;

chiyembekezo cha uchimo chionongeka.

8 Wolungama apulumuka kuvuto;

woipa nalowa m’malo mwake.

9 Wonyoza Mulungu aononga mnzake ndi m’kamwa mwake;

koma olungama adzapulumuka pakudziwa.

10 Olungama akapeza bwino, mzinda usekera;

nufuula pakuonongeka oipa.

11 Madalitso a olungama akuza mzinda;

koma m’kamwa mwa oipa muupasula.

12 Wopeputsa mnzake asowa nzeru;

koma wozindikira amatonthola.

13 Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi;

koma wokhulupirika mtima abisa mau.

14 Popanda upo wanzeru anthu amagwa;

koma pochuluka aphungu pali chipulumutso.

15 Woperekera mlendo chikole adzaphwetekwapo;

koma wakuda chikole akhala ndi mtendere.

16 Mkazi wodekha agwiritsa ulemu;

aukali nagwiritsa chuma.

17 Wachifundo achitira moyo wake zokoma;

koma wankhanza avuta nyama yake.

18 Woipa alandira malipiro onyenga;

koma wofesa chilungamo aonadi mphotho.

19 Wolimbikira chilungamo alandira moyo;

koma wolondola zoipa adzipha yekha.

20 Okhota mtima anyansa Yehova;

koma angwiro m’njira zao amsekeretsa.

21 Zoonadi, wochimwa sadzapulumuka chilango;

koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.

22 Monga chipini chagolide m’mphuno ya nkhumba,

momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.

23 Chifuniro cha olungama chifikitsa zabwino zokha;

koma chiyembekezo cha oipa mkwiyo.

24 Alipo wogawira, nangolemerabe;

aliponso womana chomwe ayenera kupatsa nangosauka.

25 Mtima wa mataya udzalemera;

wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

26 Womana tirigu anthu amtemberera;

koma madalitso adzakhala pamutu pa wogulitsa.

27 Wopwaira ubwino afunitsa chikondwerero;

koma zoipa zidzamfikira wozilondola.

28 Wokhulupirira chuma chake adzagwa;

koma olungama adzaphuka ngati tsamba.

29 Wovuta banja lake adzalowa m’zomsautsa;

wopusa adzatumikira wanzeru.

30 Chipatso cha wolungama ndi mtengo wa moyo;

ndipo wokola mtima ali wanzeru.

31 Taonani, wolungama adzalandira mphotho kunja kuno;

koposa kotani woipa ndi wochimwa?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/11-3a2dfc12137683cdafeb18a644d55365.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 12

1 Wokonda mwambo akonda kudziwa;

koma wakuda chidzudzulo apulukira.

2 Yehova akomera mtima munthu wabwino;

koma munthu wa ziwembu amtsutsa.

3 Munthu sadzakhazikika ndi udyo,

muzu wa olungama sudzasunthidwa.

4 Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wake;

koma wochititsa manyazi akunga chovunditsa mafupa a mwamunayo.

5 Maganizo a olungama ndi chiweruzo;

koma uphungu wa oipa unyenga.

6 Mau a oipa abisalira mwazi;

koma m’kamwa mwa olungama muwalanditsa.

7 Oipa amagwa kuli zii;

koma banja la olungama limaimabe.

8 Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yake;

koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9 Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,

aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10 Wolungama asamalira moyo wa choweta chake;

koma chifundo cha oipa ndi nkhanza.

11 Zakudya zikwanira wolima minda yake;

koma wotsata anthu opanda pake asowa nzeru.

12 Woipa akhumba chokodwa ndi amphulupulu;

koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13 M’kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;

koma wolungama amatuluka m’mavuto.

14 Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m’kamwa mwake;

zochita za manja ake zidzabwezedwa kwa iye.

15 Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake;

koma wanzeru amamvera uphungu.

16 Mkwiyo wa chitsiru udziwika posachedwa;

koma wanzeru amabisa manyazi.

17 Wolankhula ntheradi aonetsa chilungamo;

koma mboni yonama imanyenga.

18 Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;

koma lilime la anzeru lilamitsa.

19 Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;

koma lilime lonama likhala kamphindi.

20 Chinyengo chili m’mitima ya oganizira zoipa;

koma aphungu a mtendere amakondwa.

21 Palibe vuto lidzagwera wolungama;

koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa.

22 Milomo yonama inyansa Yehova;

koma ochita ntheradi amsekeretsa.

23 Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa;

koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.

24 Dzanja la akhama lidzalamulira;

koma waulesi adzakhala ngati kapolo.

25 Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu;

koma mau abwino aukondweretsa.

26 Wolungama atsogolera mnzake;

koma njira ya oipa iwasokeretsa.

27 Waulesi samaotcha nyama yake anaigwira;

koma wolungama amalandira chuma chopambana cha anthu.

28 M’khwalala la chilungamo muli moyo;

m’njira ya mayendedwe ake mulibe imfa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/12-a208f60d659d30d94ba0fd02c30d5dc5.mp3?version_id=1068—