Categories
MASALIMO

MASALIMO 144

Davide ayamika Mulungu kuti anamtchinjiriza, napempha ampulumutse kuti anthu adalenso

Salimo la Davide.

1 Wolemekezeka Yehova thanthwe langa,

wakuphunzitsa manja anga achite nkhondo,

zala zanga zigwirane nao:

2 Ndiye chifundo changa, ndi linga langa,

msanje wanga, ndi Mpulumutsi wanga;

chikopa changa, ndi Iye amene ndimtama;

amene andigonjetsera anthu anga.

3 Yehova, munthu ndani kuti mumdziwa?

Mwana wa munthu kuti mumsamalira?

4 Munthu akunga mpweya;

masiku ake akunga mthunzi wopitirira.

5 Weramutsani thambo lanu, Yehova, nimutsike:

Khudzani mapiri ndipo adzafuka.

6 Ng’animitsani mphezi, ndi kuwabalalitsa;

tumizani mivi yanu, ndi kuwapirikitsa.

7 Tulutsani manja anu kuchokera m’mwamba;

ndikwatuleni ndi kundilanditsa kumadzi aakulu,

kudzanja la alendo;

8 amene pakamwa pao alankhula zachabe,

ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lachinyengo.

9 Ndidzakuimbirani nyimbo yatsopano, Mulungu;

pa chisakasa cha zingwe khumi ndidzaimbira zakukulemekezani.

10 Ndiye amene apatsa mafumu chipulumutso:

Amene alanditsa Davide mtumiki wake kulupanga loipa.

11 Ndilanditseni ndi kundipulumutsa kudzanja la alendo,

amene pakamwa pao alankhula zachabe,

ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lachinyengo.

12 Kuti ana athu aamuna akhale ngati mmera udakula usanakhwime;

ana athu aakazi ngati nsanamira za kungodya,

zosema zikometsere nyumba ya mfumu.

13 Kuti nkhokwe zathu zidzale, kutipatsa za mitundumitundu;

ndi kuti nkhosa zathu ziswane zikwizikwi, inde zikwi khumi kubusako.

14 Kuti ng’ombe zathu zikhale zosenza katundu;

ndi kuti pasakhale kupasula linga kapena kutulukamo,

pasakhalenso kufuula m’makwalala athu.

15 Odala anthu akuona zotere;

odala anthu amene Mulungu wao ndi Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/144-9253b4113173caad0bef2b5147452584.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 145

Ukulu ndi ukoma wa Mulungu

Salimo lolemekeza; la Davide.

1 Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu;

ndipo ndidzalemekeza dzina lanu kunthawi za nthawi.

2 Masiku onse ndidzakuyamikani;

ndi kulemekeza dzina lanu kunthawi za nthawi.

3 Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;

ndi ukulu wake ngwosasanthulika.

4 Mbadwo wina udzalemekezera ntchito zanu mbadwo unzake,

ndipo udzalalikira zamphamvu zanu.

5 Ndidzalingalira ulemerero waukulu wa ulemu wanu,

ndi ntchito zanu zodabwitsa.

6 Ndipo adzanenera mphamvu za ntchito zanu zoopsa;

ndi ukulu wanu ndidzaufotokozera.

7 Adzabukitsa chikumbukiro cha ubwino wanu waukulu,

nadzaimbira chilungamo chanu.

8 Yehova ndiye wachisomo, ndi wachifundo;

osakwiya msanga, ndi wa chifundo chachikulu.

9 Yehova achitira chokoma onse;

ndi nsoni zokoma zake zigwera ntchito zake zonse.

10 Ntchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova;

ndi okondedwa anu adzakulemekezani.

11 Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu,

adzalankhulira mphamvu yanu.

12 Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zake,

ndi ulemerero waukulu wa ufumu wake.

13 Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya,

ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonseyonse.

14 Yehova agwiriziza onse akugwa,

naongoletsa onse owerama.

15 Maso a onse ayembekeza Inu;

ndipo muwapatsa chakudya chao m’nyengo zao.

16 Muolowetsa dzanja lanu,

nimukwaniritsira zamoyo zonse chokhumba chao.

17 Yehova ali wolungama m’njira zake zonse,

ndi wachifundo m’ntchito zake zonse.

18 Yehova ali pafupi ndi onse akuitanira kwa Iye,

onse akuitanira kwa Iye m’choonadi.

19 Adzachita chokhumba iwo akumuopa;

nadzamva kufuula kwao, nadzawapulumutsa.

20 Yehova asunga onse akukondana naye;

koma oipa onse adzawaononga.

21 Pakamwa panga padzanena chilemekezo cha Yehova;

ndi zinthu zonse zilemekeze dzina lake loyera

kunthawi za nthawi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/145-1717429a59961e0a42ee09b207785c43.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 146

Chifooko cha munthu, chikhulupiriko cha Mulungu

1 Aleluya;

Ulemekeze Yehova, moyo wanga.

2 Ndidzalemekeza Yehova m’moyo mwanga;

ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.

3 Musamakhulupirira zinduna,

kapena mwana wa munthu, amene mulibe chipulumutso mwa iye.

4 Mpweya wake uchoka, abwerera kunka kunthaka yake;

tsiku lomwelo zotsimikiza mtima zake zitayika.

5 Wodala munthu amene akhala naye

Mulungu wa Yakobo kuti amthandize,

chiyembekezo chake chili pa Yehova, Mulungu wake.

6 Amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi,

nyanja ndi zonse zili m’mwemo.

Ndiye wakusunga choonadi kosatha,

7 ndiye wakuchitira chiweruzo osautsika;

ndiye wakupatsa anjala chakudya;

Yehova amasula akaidi.

8 Yehova apenyetsa osaona;

Yehova aongoletsa onse owerama;

Yehova akonda olungama.

9 Yehova asunga alendo;

agwiriziza mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye;

koma akhotetsa njira ya oipa.

10 Yehova adzachita ufumu kosatha,

Mulungu wako,Ziyoni, ku mibadwomibadwo.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/146-682faa55b24b87d18539b47852aa329c.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 147

Alemekeze dzina la Mulungu chifukwa cha zokoma amachitira anthu ake

1 Aleluya; Pakuti kuimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma;

pakuti chikondweretsa ichi, chilemekezo chiyenera.

2 Yehova amangaYerusalemu;

asokolotsa otayika a Israele.

3 Achiritsa osweka mtima,

namanga mabala ao.

4 Awerenga nyenyezi momwe zili;

azitcha maina zonsezi.

5 Ambuye wathu ndi wamkulu ndi wa mphamvu zambiri;

nzeru yake njosatha.

6 Yehova agwiriziza ofatsa;

atsitsira oipa pansi.

7 Yamikani Yehova ndi kuthira mang’ombe;

muimbireni Mulungu wathu zomlemekeza pazeze:

8 Amene aphimba thambo ndi mitambo,

amene akonzera mvula nthaka,

amene aphukitsa msipu pamapiri.

9 Amene apatsa zoweta chakudya chao,

ana a khwangwala alikulira.

10 Mphamvu ya kavalo siimkonda:

Sakondwera nayo miyendo ya munthu.

11 Yehova akondwera nao akumuopa Iye,

iwo akuyembekeza chifundo chake.

12 Yerusalemu, lemekezani Yehova;

Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu.

13 Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu:

Anadalitsa ana anu m’kati mwanu.

14 Ndiye amene akhalitsa malire anu mumtendere;

akukhutitsani ndi tirigu wakucha bwino.

15 Atumiza lamulo lake kudziko lapansi;

mau ake athamanga liwiro.

16 Apatsa chipale chofewa ngati ubweya;

awaza chisanu ngati phulusa.

17 Aponya matalala ake ngati zidutsu:

Adzaima ndani pa kuzizira kwake?

18 Atumiza mau ake nazisungunula;

aombetsa mphepo yake, ayenda madzi ake.

19 Aonetsa mau ake kwa Yakobo;

malemba ake, ndi maweruzo ake kwa Israele.

20 Sanatero nao anthu a mtundu wina;

ndipo za maweruzo ake, sanawadziwe.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/147-908d9874eb731e84402030f8fb68f978.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 148

Zolengedwa zonse zilemekeze Mulungu

1 Aleluya.

Lemekezani Yehova kochokera kumwamba;

mlemekezeni m’misanje.

2 Mlemekezeni,angeloake onse;

mlemekezeni, makamu ake onse.

3 Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi;

mlemekezeni, nyenyezi zonse zounikira.

4 Mlemekezeni, m’mwambamwamba,

ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.

5 Alemekeze dzina la Yehova;

popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

6 Anazikhazikanso kunthawi za nthawi;

anazipatsa chilamulo chosatumphika.

7 Lemekezani Yehova kochokera ku dziko lapansi,

zinsomba inu, ndi malo ozama onse;

8 moto ndi matalala, chipale chofewa ndi nkhungu;

mphepo ya namondwe, yakuchita mau ake;

9 mapiri ndi zitunda zonse;

mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:

10 Nyama zakuthengo ndi zoweta zonse;

zokwawa, ndi mbalame zakuuluka.

11 Mafumu a padziko ndi mitundu yonse ya anthu;

zinduna ndi oweruza onse a padziko.

12 Anyamata ndiponso anamwali;

okalamba pamodzi ndi ana.

13 Alemekeze dzina la Yehova;

pakuti dzina lake lokha ndi lokwezeka;

ulemerero wake uli pamwamba padziko lapansi ndi thambo.

14 Ndipo anakweza nyanga ya anthu ake,

chilemekezo cha okondedwa ake onse;

ndiwo ana a Israele, anthu a pafupi pa Iye.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/148-c66f417a2811e794129a4da622dd16f6.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 149

Okhulupirira onse alemekeze Mulungu wao

1 Aleluya,

Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano,

ndi chilemekezo chake mu msonkhano wa okondedwa ake.

2 Akondwere Israele mwa Iye amene anamlenga;

ana aZiyoniasekere mwa mfumu yao.

3 Alemekeze dzina lake ndi kuthira mang’ombe;

amuimbire zomlemekeza ndi lingaka ndi zeze.

4 Popeza Yehova akondwera nao anthu ake;

adzakometsa ofatsa ndi chipulumutso.

5 Okondedwa ake atumphe mokondwera mu ulemu:

Afuule mokondwera pamakama pao.

6 Nyimbo zakukweza Mulungu zikhale pakamwa pao,

ndi lupanga lakuthwa konsekonse m’dzanja lao;

7 kubwezera chilango akunja,

ndi kulanga mitundu ya anthu;

8 kumanga mafumu ao ndi maunyolo,

ndi omveka ao ndi majerejede achitsulo,

9 kuwachitira chiweruzo cholembedwacho.

Ulemu wa okondedwa ake onse ndi uwu.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/149-b1b2c40a110f35b6860b2e347ecb0dc0.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 150

Zolengedwa zonse zilemekeze Mulungu

1 Aleluya.

Lemekezani Mulungu m’malo ake oyera;

mlemekezeni m’thambo la mphamvu yake.

2 Mlemekezeni chifukwa cha ntchito zake zolimba;

mlemekezeni monga mwa ukulu wake waunjinji.

3 Mlemekezeni ndi kulira kwa lipenga;

mlemekezeni ndi chisakasa ndi zeze.

4 Mlemekezeni ndi lingaka ndi kuthira mang’ombe:

Mlemekezeni ndi zoimbira za zingwe ndi chitoliro.

5 Mlemekezeni ndi nsanje zomveka:

Mlemekezeni ndi nsanje zoliritsa.

6 Zonse zakupuma zilemekeze Yehova.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/150-cc3e9fddf631e35069b3094bda171bd4.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli liphunzitsa nzeru zosiyanasiyana zothandiza anthu ndi kuwongolera moyo wao wa masiku onse mwa njira yokomera Mulungu ndi anzao. Mau ake ambiri akuwoneka ngati miyambi. Mau oyamba akuti, “Kudziwa nzeru ndi mwambo; kuzindikira mau ozindikiritsa; kulandira mwambo wakusamalira machitidwe, chilungamo, chiweruzo ndi zolunjika.” Kenaka bukuli likupereka malangizo osiyanasiyana okhudza makhalidwe, kusunga mwambo, kupatsana ulemu ndi kukhalirana mwamtendere, kutsata choona ndi chilungamo, moyo wa pa banja, pa ntchito, pa malonda, pa maphwando ndi pa zochitika zina zilizonse. Nzeru ndizo zimene akuluakulu a Israele ankaphunzitsa anthu ao pa masiku akale. Wofuna kutsata nzeruzo ayenera kudzilamulira, kudzichepetsa, kuleza mtima, kulemekeza osauka ndi kukhala okhulupirika pa chibwenzi.

Za mkatimu

Bukuli lili ndi zigawo zingapo:

Mau oyamikira nzeru

1.1—9.18

Miyambi ya Solomoni

10.1—29.27

Mau a Aguri

30.1-33

Mau ena osiyanasiyana

31.1-31

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 1

Zochitira miyambo

1 Miyambo ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israele.

2 Kudziwa nzeru ndi mwambo;

kuzindikira mau ozindikiritsa;

3 kulandira mwambo wakusamalira machitidwe,

chilungamo, chiweruzo ndi zolunjika;

4 kuchenjeza achibwana,

kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;

5 kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira;

ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;

6 kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lake,

mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.

Munthu asalole oipa amchete

7 Kuopa Yehova ndiko chiyambi cha kudziwa;

opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

8 Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,

ndi kusasiya chilangizo cha amai ako;

9 pakuti izi ndi korona wa chisomo pamutu pako,

ndi mkanda pakhosi pako.

10 Mwananga, akakukopa ochimwa usalole.

11 Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi,

tilalire osachimwa opanda chifukwa;

12 tiwameze ali ndi moyo ngati manda,

ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;

13 tidzapeza chuma chonse cha mtengo wake,

tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;

14 udzachita nafe maere,

tonse tidzakhala ndi chotengeramo chimodzi.

15 Mwananga, usayende nao m’njira;

letsa phazi lako ku mayendedwe ao;

16 pakuti mapazi ao athamangira zoipa,

afulumira kukhetsa mwazi.

17 Pakuti kutchera msampha pamaso pa mbalame ndi chabe;

18 ndipo awa abisalira mwazi waowao, alalira miyoyo yaoyao.

19 Mayendedwe a yense wopindula chuma monyenga ngotere;

chilanda moyo wa eni ake.

Chenjezo la Nzeru

20 Nzeru ifuula panja;

imveketsa mau ake pabwalo;

21 iitana posonkhana anthu polowera pachipata;

m’mzinda inena mau ake,

22 Kodi mudzakonda zazibwana kufikira liti, achibwana inu?

Onyoza ndi kukonda kunyoza,

opusa ndi kuda nzeru?

23 Tembenukani pamene ndikudzudzulani;

taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga,

ndikudziwitsani mau anga.

24 Chifukwa ndaitana, ndipo munakana;

ndatambasula dzanja langa,

ndipo panalibe analabadira;

25 koma munapeputsa uphungu wanga wonse,

ndi kukana kudzudzula kwanga.

26 Inetu ndidzachitira chiphwete tsoka lanu,

ndidzatonyola pakudza mantha anu;

27 pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,

ndi pofika tsoka lanu ngati kamvulumvulu;

pakudza kwa inu vuto ndi nsautso.

28 Pamenepo adzandiitana,

koma sindidzavomera;

adzandifunatu, osandipeza ai;

29 chifukwa anada nzeru,

sanafune kuopa Yehova;

30 anakana uphungu wanga,

nanyoza kudzudzula kwanga konse;

31 momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao,

nadzakhuta zolingalira zao.

32 Pakuti kubwerera m’mbuyo kwa achibwana kudzawapha;

ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.

33 Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka,

nadzakhala phee osaopa zoipa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/1-32cef618ad9ecae5edf89bcb3338ccd7.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 2

Ukoma ndi phindu lake la Nzeru

1 Mwananga, ukalandira mau anga,

ndi kusunga malamulo anga;

2 kutcherera makutu ako kunzeru,

kulozetsa mtima wako kukuzindikira;

3 ukaitananso luntha,

ndi kufuulira kuti ukazindikire;

4 ukaifunafuna ngatisiliva,

ndi kuipwaira ngati chuma chobisika;

5 pompo udzazindikira kuopa Yehova

ndi kumdziwadi Mulungu.

6 Pakuti Yehova apatsa nzeru;

kudziwa ndi kuzindikira kutuluka m’kamwa mwake.

7 Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni;

ndiye chikopa cha oyenda molunjika;

8 kuti atchinjirize njira za chiweruzo,

nadikire khwalala la opatulidwa ake.

9 Pamenepo udzazindikira chilungamo ndi chiweruzo,

zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.

10 Pakuti nzeru idzalowa m’mtima mwako,

moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

11 kulingalira kudzakudikira,

kuzindikira kudzakutchinjiriza;

12 kukupulumutsa kunjira yoipa,

kwa anthu onena zokhota;

13 akusiya mayendedwe olungama,

akayende m’njira za mdima;

14 omwe asangalala pochita zoipa,

nakondwera ndi zokhota zoipa;

15 amene apotoza njira zao,

nakhotetsa mayendedwe ao.

16 Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi wachiwerewere,

kwa mkazi wachilendo wosyasyalika ndi mau ake;

17 wosiya bwenzi la ubwana wake,

naiwalachipanganocha Mulungu wake.

18 Nyumba yake itsikira kuimfa,

ndi mayendedwe ake kwa akufa;

19 onse akunka kwa iye sabweranso,

safika kunjira za moyo;

20 nzeru idzakuyendetsa m’njira ya anthu abwino,

kuti usunge mayendedwe a olungama.

21 Pakuti oongoka mtima adzakhala m’dziko,

angwiro nadzatsalamo.

22 Koma oipa adzalikhidwa m’dziko,

achiwembu adzazulidwamo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/2-cf23f208ad1a7192340fc8e2c2fe8d53.mp3?version_id=1068—