Categories
MASALIMO

MASALIMO 134

Afulumizidwa anthu kulemekeza Yehova

Nyimbo yokwerera.

1 Taonani, lemekezani Yehova, atumiki a Yehova inu nonse,

akuimirira m’nyumba ya Yehova usiku.

2 Kwezani manja anu kumalo oyera,

nimulemekeze Yehova.

3 Yehova, ali muZiyoni, akudalitseni;

ndiye amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/134-c0ab6cf3799896400acd612283803b61.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 135

Mulungu alemekezedwa pa ukulu wake. Mafano ndi achabe

1 Aleluya; Lemekezani dzina la Yehova!

Lemekezani inu atumiki a Yehova.

2 Inu akuimirira m’nyumba ya Yehova,

m’mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

3 Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino;

muimbire zolemekeza dzina lake; pakuti nkokondweretsa kutero.

4 Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo,

Israele, akhale chuma chake chenicheni.

5 Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkulu,

ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.

6 Chilichonse chimkonda Yehova achichita,

kumwamba ndi padziko lapansi, m’nyanja ndi mozama monse.

7 Akweza mitambo ichokere ku malekezero a dziko lapansi;

ang’animitsa mphezi zidzetse mvula;

atulutsa mphepo mosungira mwake.

8 Anapanda oyamba a Ejipito,

kuyambira munthu kufikira zoweta.

9 Anatumiza zizindikiro ndi zodabwitsa pakati pako, Ejipito iwe,

paFaraondi pa omtumikira onse.

10 Ndiye amene anapandaamitunduambiri,

napha mafumu amphamvu;

11 Sihoni mfumu ya Aamori,

ndi Ogi mfumu ya Basani,

ndi maufumu onse a Kanani:

12 Ndipo anapereka dziko lao likhale cholowa,

cholowa cha kwa Israele anthu ake.

13 Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;

chikumbukiro chanu, Yehova, kufikira mibadwomibadwo.

14 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake,

koma adzaleka atumiki ake.

15 Mafano a amitundu ndiwosilivandi golide,

ntchito ya manja a anthu.

16 Pakamwa ali napo koma osalankhula;

maso ali nao, koma osapenya;

17 makutu ali nao, koma osamva;

inde, pakamwa pao palibe mpweya.

18 Akuwapanga adzafanana nao;

inde, onse akuwakhulupirira.

19 A nyumba ya Israele inu, lemekezani Yehova:

A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:

20 A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova:

Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.

21 Alemekezedwe Yehova kuchokera muZiyoni,

amene akhala muYerusalemu.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/135-17e07ebb8041dcceaa116f59e06f9179.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 136

Mulungu alemekezedwe pa chifundo chake

1 Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino;

pakuti chifundo chake nchosatha.

2 Yamikani Mulungu wa milungu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

3 Yamikani Mbuye wa ambuye;

pakuti chifundo chake nchosatha.

4 Amene yekha achita zodabwitsa zazikulu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

5 Amene analenga zakumwamba mwanzeru;

pakuti chifundo chake nchosatha.

6 Amene anayala dziko lapansi pamwamba pamadzi;

pakuti chifundo chake nchosatha.

7 Amene analenga miuni yaikulu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

8 Dzuwa liweruze usana;

pakuti chifundo chake nchosatha.

9 Mwezi ndi nyenyezi ziweruze usiku;

pakuti chifundo chake nchosatha.

10 Iye amene anapandira Aejipito ana ao oyamba;

pakuti chifundo chake nchosatha.

11 Natulutsa Israele pakati pao;

pakuti chifundo chake nchosatha.

12 Ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka;

pakuti chifundo chake nchosatha.

13 Amene anagawa magawo Nyanja Yofiira;

pakuti chifundo chake nchosatha.

14 Napititsa Israele pakati pake;

pakuti chifundo chake nchosatha.

15 NakhuthulaFaraondi khamu lake mu Nyanja Yofiira:

pakuti chifundo chake nchosatha.

16 Amene anatsogolera anthu ake m’chipululu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

17 Amene anapanda mafumu aakulu;

pakuti chifundo chake nchosatha.

18 Ndipo anawapha mafumu omveka;

pakuti chifundo chake nchosatha.

19 Sihoni mfumu ya Aamori;

pakuti chifundo chake nchosatha.

20 Ndi Ogi mfumu ya Basani;

pakuti chifundo chake nchosatha.

21 Ndipo anapereka dziko lao likhale cholowa;

pakuti chifundo chake nchosatha.

22 Cholowa cha kwa Israele mtumiki wake;

pakuti chifundo chake nchosatha.

23 Amene anatikumbukira popepuka ife;

pakuti chifundo chake nchosatha.

24 Natikwatula kwa otisautsa;

pakuti chifundo chake nchosatha.

25 Ndiye wakupatsa nyama zonse chakudya;

pakuti chifundo chake nchosatha.

26 Yamikani Mulungu wa Kumwamba,

pakuti chifundo chake nchosatha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/136-3ce0d50841b7431da42362b695c5d946.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 137

Kudandaula kwa Ayuda ku Babiloni

1 Ku mitsinje ya ku Babiloni,

kumeneko tinakhala pansi, inde tinalira,

pokumbukiraZiyoni.

2 Pa msondodzi uli m’mwemo

tinapachika mazeze athu.

3 Popeza pamenepo akutigwirawo anatifunsa nyimbo

ndipo akutizunza anafuna tisekere,

ndi kuti, Mutiimbire nyimbo imodzi ya ku Ziyoni.

4 Tidati, Tidzaimba bwanji nyimbo ya Yehova

m’dziko lachilendo?

5 Ndikakuiwalani, Yerusalemu,

dzanja lamanja langa liiwale luso lake.

6 Lilime langa limamatike kunsaya zanga,

ndikapanda kukumbukira inu;

ndikapanda kusankha Yerusalemu

koposa chimwemwe changa chopambana.

7 Yehova, kumbukirani ana a Edomu

tsiku la Yerusalemu;

amene adati, Gamulani, gamulani,

kufikira maziko ake.

8 Mwana wamkazi wa ku Babiloni,

iwe amene udzapasulidwa;

wodala iye amene adzakubwezera chilango

monga umo unatichitira ife.

9 Wodala iye amene adzagwira makanda ako,

ndi kuwaphwanya pathanthwe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/137-ebdfdfe95ab47203bfc2919fabb5e2db.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 138

Davide ayamika Mulungu pa kukhulupirika kwake, naneneratu kuti mafumu onse adzatero

Salimo la Davide.

1 Ndidzakuyamikani ndi mtima wanga wonse;

ndidzaimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu.

2 Ndidzagwadira kuloza ku Kachisi wanu woyera,

ndi kuyamika dzina lanu,

chifukwa cha chifundo chanu ndi choonadi chanu;

popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

3 Tsiku loitana ine, munandiyankha,

munandilimbitsa ndi mphamvu m’moyo mwanga.

4 Mafumu onse a padziko lapansi adzakuyamikani,

Yehova, popeza adamva mau a pakamwa panu.

5 Ndipo adzaimbira njira za Yehova;

pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

6 Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo;

koma wodzikuza amdziwira kutali.

7 Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo;

mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu,

ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.

8 Yehova adzanditsirizira za kwa ine:

Chifundo chanu, Yehova, chifikira kunthawi zonse:

Musasiye ntchito za manja anu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/138-baf99d1c1610bf2b5dde57b52d513be1.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 139

Mulungu ali ponseponse, adziwa zonse

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la Davide.

1 Munandisanthula, Yehova, nimundidziwa.

2 Inu mudziwa kukhala kwanga ndi kuuka kwanga,

muzindikira lingaliro langa muli kutali.

3 Muyesa popita ine ndi pogona ine,

ndi njira zanga zonse muzolowerana nazo.

4 Pakuti asanafike mau pa lilime langa,

taonani, Yehova, muwadziwa onse.

5 Munandizinga kumbuyo ndi kumaso,

nimunaika dzanja lanu pa ine.

6 Kudziwa ichi kundiposa ndi kundidabwitsa:

Kundikhalira patali, sindifikirako.

7 Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu?

Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu?

8 Ndikakwera kunka kumwamba, muli komweko;

kapena ndikadziyalira kuGehena, taonani, muli komweko.

9 Ndikadzitengera mapiko a mbandakucha,

ndi kukhala ku malekezero a nyanja;

10 kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera,

nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.

11 Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe,

ndi kuunika kondizinga kukhale usiku.

12 Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu,

koma usiku uwala ngati usana;

mdima ukunga kuunika.

13 Pakuti Inu munalenga impso zanga;

munandiumba ndisanabadwe ine.

14 Ndikuyamikani chifukwa kuti chipangidwe changa

nchoopsa ndi chodabwitsa;

ntchito zanu nzodabwitsa;

moyo wanga uchidziwa ichi bwino ndithu.

15 Thupi langa silinabisikire Inu popangidwa ine mobisika,

poombedwa ine monga m’munsi mwake mwa dziko lapansi.

16 Ndisanaumbidwe ine maso anu anandipenya,

ziwalo zanga zonse zinalembedwa m’buku mwanu,

masiku akuti ziumbidwe,

pakalibe chimodzi cha izo.

17 Potero, Mulungu, ndiziyesa zolingalira zanu za mtengo wake ndithu!

Mawerengedwe ake ndi ambirimbiri!

18 Ndikaziwerenga zichuluka koposa mchenga:

Ndikauka ndikhalanso nanu.

19 Indedi, mudzaomba woipa, Mulungu:

Ndipo amuna inu okhumba mwazi, chokani kwa ine.

20 Popeza anena za Inu moipa,

ndi adani anu atchula dzina lanu mwachabe.

21 Kodi sindidana nao iwo akudana ndi Inu, Yehova?

Ndipo kodi sindimva nao chisoni iwo akuukira Inu?

22 Ndidana nao ndi udani weniweni,

ndiwayesa adani.

23 Mundisanthule, Mulungu, nimudziwe mtima wanga;

mundiyese nimudziwe zolingalira zanga.

24 Ndipo mupenye ngati ndili nao mayendedwe oipa,

nimunditsogolere panjira yosatha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/139-1027ada5dc3d0158a17f5a9160443273.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 140

Davide apempha Mulungu amlanditse kwa mdani woipa wamphamvu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la Davide.

1 Ndilanditseni, Yehova, kwa munthu woipa;

ndisungeni kwa munthu wachiwawa;

2 amene adzipanga zoipa mumtima mwao;

masiku onse amemeza nkhondo.

3 Anola lilime lao ngati njoka;

pansi pa milomo yao pali ululu wa mphiri.

4 Ndilindireni Yehova, ndisalowe m’manja mwa woipa;

ndisungeni kwa munthu wachiwawa;

kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.

5 Odzikuza ananditchera msampha, nandibisira zingwe;

anatcha ukonde m’mphepete mwa njira;

ananditchera makwekwe.

6 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga;

munditcherere khutu mau a kupemba kwanga, Yehova.

7 Yehova Ambuye, ndinu mphamvu ya chipulumutso changa,

munandiphimba mutu wanga tsiku lakulimbana nkhondo.

8 Yehova, musampatse woipa zokhumba iye;

musamthandize zodzipanga zake; angadzikuze.

9 Kunena za mutu wao wa iwo akundizinga,

choipa cha milomo yao chiwaphimbe.

10 Makala amoto awagwere;

aponyedwe kumoto;

m’maenje ozama, kuti asaukenso.

11 Munthu wamlomo sadzakhazikika padziko lapansi;

choipa chidzamsaka munthu wachiwawa kuti chimgwetse.

12 Ndidziwa kuti Yehova adzanenera wozunzika mlandu,

ndi kuweruzira aumphawi.

13 Indedi, olungama adzayamika dzina lanu;

oongoka mtima adzakhala pamaso panu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/140-f00ee044309bcb1491e964d9efe48d2e.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 141

Davide apempha Mulungu amthandize poyesedwa ndi zoipa

Salimo la Davide.

1 Yehova, ndaitana kwa Inu; ndifulumireni ine;

munditcherere khutu, pamene ndiitana kwa Inu.

2 Pemphero langa liikike ngati chofukiza pamaso panu;

kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.

3 Muike mdindo pakamwa panga, Yehova;

sungani pakhomo pa milomo yanga.

4 Mtima wanga usalinge kuchinthu choipa,

kuchita ntchito zoipa

ndi anthu akuchita zopanda pake;

ndipo ndisadye zankhuli zao.

5 Akandipanda munthu wolungama ndidzati nchifundo:

akandidzudzula, ndidzakuyesa mafuta a pamutu;

mutu wanga usakane:

Pakuti pangakhale posautsidwa iwo ndidzawapempherera.

6 Oweruza ao anagwetseka pambali pa thanthwe;

nadzamva mau anga kuti ndiwo okondweretsa.

7 Mafupa athu amwazika pakamwa pa manda,

monga ngati akumba nanyimphula nthaka yapansi.

8 Pakuti maso anga apenya kwanu, Yehova Ambuye;

ndithawira kwa Inu; musataye moyo wanga.

9 Mundisunge ndisagwe mumsampha ananditcherawo,

ndisakodwe m’makwekwe a iwo ochita zopanda pake.

10 Oipa agwe pamodzi m’maukonde ao,

kufikira nditapitirira ine.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/141-36576f5f05d631c1d64279db9e575199.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 142

Pemphero pakuopsedwa kwakukulu

Chilangizo cha Davide, muja anakhala m’phanga; Pemphero.

1 Ndifuula nalo liu langa kwa Yehova;

ndi mau anga ndipemba kwa Yehova.

2 Nditsanulira kudandaula kwanga pamaso pake;

ndionetsa msauko wanga pamaso pake.

3 Pamene mzimu wanga unakomoka m’kati mwanga, munadziwa njira yanga.

M’njira ndiyendamo ananditchera msampha.

4 Penyani kudzanja lamanja ndipo muone; palibe wondidziwa;

pothawirapo pandisowa; palibe mmodzi wosamalira moyo wanga.

5 Ndinafuulira kwa inu, Yehova;

ndinati, Inu ndinu pothawirapo panga,

gawo langa m’dziko la amoyo.

6 Tamverani kufuula kwanga; popeza ndisauka kwambiri;

ndilanditseni kwa iwo akundilondola; popeza andipambana.

7 Tulutsani moyo wanga m’ndende, kuti ndiyamike dzina lanu;

olungama adzandizinga;

pakuti mudzandichitira zokoma.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/142-4d4719bacbb778eb570fed3078acd2bf.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 143

Davide apempha Mulungu amlanditse msanga kwa adani ake

Salimo la Davide.

1 Imvani pemphero langa, Yehova; nditcherere khutu kupemba kwanga;

ndiyankheni mwa chikhulupiriko chanu, mwa chilungamo chanu.

2 Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu;

pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.

3 Pakuti mdani alondola moyo wanga;

apondereza pansi moyo wanga;

andikhalitsa mumdima monga iwo adafa kale lomwe.

4 Potero mzimu wanga wakomoka mwa ine;

mtima wanga utenga nkhawa m’kati mwanga.

5 Ndikumbukira masiku a kale lomwe;

zija mudazichita ndilingirirapo;

ndikamba pandekha za ntchito ya manja anu.

6 Nditambalitsira manja anga kwa Inu:

Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.

7 Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha.

Musandibisire nkhope yanu;

ndingafanane nao akutsikira kudzenje.

8 Mundimvetse chifundo chanu mamawa;

popeza ndikhulupirira Inu:

Mundidziwitse njira ndiyendemo;

popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

9 Mundilanditse kwa adani anga, Yehova;

ndibisala mwa Inu.

10 Mundiphunzitse chokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kuchidikha.

11 Mundipatse moyo, Yehova, chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu mutulutse moyo wanga m’sautso.

12 Ndipo mwa chifundo chanu mundidulire adani anga,

ndipo muononge onse akusautsa moyo wanga;

pakuti ine ndine mtumiki wanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/143-c4534d5452662442eac4ab35bfdad210.mp3?version_id=1068—