Categories
MASALIMO

MASALIMO 124

Mulungu yekha walanditsa anthu ake

Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Akadapanda kukhala nafe Yehova,

anene tsono Israele;

2 Akadapanda kukhala nafe Yehova,

pakutiukira anthu:

3 Akadatimeza amoyo,

potipsera mtima wao.

4 Akadatimiza madziwo,

mtsinje ukadapita pa moyo wathu;

5 madzi odzikuza akadapita pa moyo wathu.

6 Alemekezedwe Yehova,

amene sanatipereke kumano kwao tikhale chakudya chao.

7 Moyo wathu unaonjoka ngati mbalame mu msampha wa msodzi;

msampha unathyoka ndi ife tinaonjoka.

8 Thandizo lathu lili m’dzina la Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/124-2ff8b83e597e46994d314767b3d637d9.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 125

Okhulupirira Yehova akhazikika mtima

Nyimbo yokwerera.

1 Iwo akukhulupirira Yehova

akunga phiri laZiyoni, losasunthika, likhazikika kosatha.

2 Monga mapiri azingaYerusalemu,

momwemo Yehova azinga anthu ake,

kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

3 Pakuti ndodo yachifumu ya choipa siidzapumula pa gawo la olungama;

kuti olungama asatulutse dzanja lao kuchita chosalungama.

4 Chitirani chokoma, Yehova, iwo okhala okoma;

iwo okhala oongoka mumtima mwao.

5 Koma iwo akupatula kutsata njira zao zokhotakhota,

Yehova adzawachotsa pamodzi ndi ochita zopanda pake.

Mtendere ukhale pa Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/125-eebef3497cf7bba78426c82c1869b5f7.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 126

Ayamikira mokondwerera kuti Mulungu anabweza ukapolo wao

Nyimbo yokwerera.

1 Pobweza Yehova ukapolo waZiyoni,

tinakhala ngati anthu akulota.

2 Pamenepo pakamwa pathu panadzala ndi kuseka,

ndi lilime lathu linafuula mokondwera;

pamenepo anati kwaamitundu,

Yehova anawachitira iwo zazikulu.

3 Yehova anatichitira ife zazikulu;

potero tikhala okondwera.

4 Bwezani ukapolo wathu, Yehova,

ngati mitsinje ya kumwera.

5 Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kufuula mokondwera.

6 Iye amene ayendayenda nalira, ponyamula mbeu yakufesa;

adzabweranso ndithu ndi kufuula mokondwera,

alikunyamula mitolo yake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/126-3263cbbe85cce41a2b4edb42773efe99.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 127

Madalitso onse, a m’banja omwe, achokera kwa Mulungu

Nyimbo yokwerera; ya Solomoni.

1 Akapanda kumanga nyumba Yehova,

akuimanga agwiritsa ntchito chabe;

akapanda kusunga mzinda Yehova,

mlonda adikira chabe.

2 Kuli chabe kwa inu kulawirira mamawa ndi kusagonerapo madzulo,

kudya mkate wosautsa kuupeza;

kuli tero kuti izi apatsa okondedwa ake ngati m’tulo.

3 Taonani, ana ndiwo cholowa cha kwa Yehova;

chipatso cha m’mimba ndicho mphotho yake.

4 Ana a ubwana wake wa munthu

akunga mivi m’dzanja lake la chiphona.

5 Wodala munthu amene anadzaza nayo phodo lake:

sadzachita manyazi iwo,

pakulankhula nao adani kuchipata.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/127-eeeab4dcd9f3f75aeebe2f4be6f88302.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 128

Wakuopa Yehova adalitsidwa m’banja mwake

Nyimbo yokwerera.

1 Wodala yense wakuopa Yehova,

wakuyenda m’njira zake.

2 Pakuti udzadya za ntchito ya manja ako;

wodala iwe, ndipo kudzakukomera.

3 Mkazi wako adzanga mpesa wopatsa m’mbali za nyumba yako;

ana ako adzanga timitengo taazitonapozinga podyera pako.

4 Taonani, m’mwemo adzadalitsika

munthu wakuopa Yehova.

5 Yehova adzakudalitsa ali muZiyoni;

ndipo udzaona zokoma zaYerusalemumasiku onse a moyo wako.

6 Inde, udzaona zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/128-8627e2c90ea4f24759ec93550f80d408.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 129

Israele asautsidwa koma osafafanizidwa

Nyimbo yokwerera.

1 Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga,

anene tsono Israele;

2 Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga;

koma sanandilake.

3 Olima analima pamsana panga;

anatalikitsa mipere yao.

4 Yehova ndiye wolungama;

anadulatu zingwe za oipa.

5 Achite manyazi nabwerere m’mbuyo.

Onse akudana nayeZiyoni.

6 Akhale ngati udzu womera patsindwi,

wakufota asanauzule;

7 umene womweta sadzaza nao dzanja lake,

kapena womanga mitolo sakupatira manja.

8 Angakhale opitirirapo sanena,

Dalitso la Mulungu likhale pa inu;

tikudalitsani m’dzina la Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/129-93250a4a1c17089c758d1fec58b2d20a.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 130

Pemphero lakuti akhululukidwe

Nyimbo yokwerera.

1 M’mozamamo ndinakufuulirani, Yehova.

2 Ambuye, imvani liu langa;

makutu anu akhale chimverere

mau a kupemba kwanga.

3 Mukasunga mphulupulu, Yehova,

adzakhala chilili ndani, Ambuye?

4 Koma kwa Inu kuli chikhululukiro,

kuti akuopeni.

5 Ndilindira Yehova, moyo wanga ulindira,

ndiyembekeza mau ake.

6 Moyo wanga uyang’anira Ambuye,

koposa alonda matanda kucha;

inde koposa alonda matanda kucha.

7 Israele, uyembekezere Yehova;

chifukwa kwa Yehova kuli chifundo,

kwaonso kuchulukira chiombolo.

8 Ndipo adzaombola Israele

ku mphulupulu zake zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/130-08ede17c17095cb89fbacd5a4d727f95.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 131

Kudzichepetsa kwa Davide pakupemphera

Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Yehova, mtima wanga sunadzikuze

ndi maso anga sanakwezeke;

ndipo sindinatsate zazikulu,

kapena zodabwitsa zondiposa.

2 Indedi, ndinalinganiza ndi kutontholetsa moyo wanga;

ngati mwana womletsa kuyamwa amake,

moyo wanga ndili nao ngati mwana womletsa kuyamwa.

3 Israele, uyembekezere Yehova,

kuyambira tsopano kufikira kosatha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/131-4a5e96ec1785b548b0bd2c780c328f05.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 132

Davide asamalira Kachisi ndi likasa. Lonjezano la Mulungu

Nyimbo yokwerera.

1 Yehova, kumbukirani Davide

kuzunzika kwake konse.

2 Kuti analumbira Yehova,

nawindira Wamphamvuyo wa Yakobo, ndi kuti,

3 Ngati ndidzalowa pakhomo pa nyumba yanga,

ngati ndidzakwera pa kama logonapo;

4 ngati ndidzalola maso anga agone,

kapena zikope zanga ziodzere;

5 kufikira nditapezera Yehova malo,

chokhalamo Wamphamvuyo wa Yakobo?

6 Taonani, tinachimva mu Efurata;

tinachipeza kuchidikha cha kunkhalango.

7 Tidzalowa mokhalamo Iye;

tidzagwadira kumpando wa mapazi ake.

8 Ukani, Yehova, lowani ku mpumulo wanu;

Inu ndi hema wa mphamvu yanu.

9 Ansembe anu avale chilungamo;

ndi okondedwa anu afuule mokondwera.

10 Chifukwa cha Davide mtumiki wanu

musabweze nkhope ya wodzozedwa wanu.

11 Yehova analumbira Davide zoona;

sadzalibweza; ndi kuti,

Wa iwo okhala zipatso za thupi lako

ndidzaika pa mpando wachifumu wako.

12 Ana ako akasungachipanganochanga

ndi mboni yanga imene ndidzawaphunzitsa,

ana aonso adzakhala pa mpando wanu kunthawi zonse,

13 pakuti Yehova anasankhaZiyoni;

analikhumba likhale pokhala pake; ndi kuti,

14 Pampumulo panga mpano posatha,

Pano ndidzakhala; pakuti ndakhumbapo.

15 Ndidzadalitsatu chakudya chake;

aumphawi ake ndidzawakhutitsa ndi mkate.

16 Ndipo ansembe ake ndidzawaveka ndi chipulumutso:

Ndi okondedwa ake adzafuulitsa mokondwera.

17 Apo ndidzaphukitsira Davide nyanga;

ndakonzeratu wodzozedwa wanga nyali.

18 Ndidzawaveka adani ake ndi manyazi;

koma pa iyeyu korona wake adzamveka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/132-1a766d8dc23c1a98cb39b86003c887b4.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 133

Chikondano cha abale ndi chokoma

Nyimbo yokwerera; ya Davide.

1 Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu

kuti abale akhale pamodzi!

2 Ndiko ngati mafuta a mtengo wake pamutu,

akutsikira kundevu,

inde kundevu za Aroni;

akutsikira kumkawo wa zovala zake.

3 Ngati mame a ku Heremoni,

akutsikira pa mapiri aZiyoni.

Pakuti pamenepo Yehova analamulira dalitsolo,

ndilo moyo womka muyaya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/133-de1654ae8ff13fcab0f2dd7436667ef5.mp3?version_id=1068—