Categories
OWERUZA

OWERUZA 3

Amitundu otsala akuyesa nao Aisraele

1 Ndipo iyo ndiyo mitundu ya anthu anaisiyapo Yehova kuyesa nayo Israele, ndiwo onse amene sanadziwe nkhondo zonse za Kanani;

2 chifukwa chake ndicho chokha chakuti adziwitse mibadwo ya ana a Israele ndi kuwaphunzitsa nkhondo, ngakhale iwo okhaokha osaidziwa konse kale;

3 anasiya mafumu asanu a Afilisti ndi Akanani onse, ndi Asidoni, ndi Ahivi okhala m’phiri la Lebanoni, kuyambira phiri la Baala-Heremoni mpaka polowera ku Hamati.

4 Amenewo anakhala choyesera Israele kuti Yehova adziwe ngati adzamvere malamulo ake, amene analamulira makolo ao mwa dzanja la Mose.

5 Ndipo ana a Israele anakhala pakati pa Akanani, Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi;

6 nakwatira ana aakazi a iwowa, napereka ana ao akazi kwa ana aamuna a iwowa natumikira milungu yao.

Otiniyeli alanditsa Aisraele m’dzanja la Kusani

7 Ndipo ana a Israele anachita choipa pamaso pa Yehova, naiwala Yehova Mulungu wao, natumikira Abaalandi zifanizo.

8 Pamenepo mkwiyo wa Yehova unayakira Israele ndipo anawagulitsa m’dzanja la Kusani-Risataimu, mfumu ya Mesopotamiya; ndi ana a Israele anatumikira Kusani-Risataimu zaka zisanu ndi zitatu.

9 Ndipo pamene ana a Israele anafuula kwa Yehova, Yehova anaukitsira ana a Israele mpulumutsi amene anawapulumutsa, ndiye Otiniyele mwana wa Kenazi, mng’ono wake wa Kalebe.

10 Ndipo unamdzera mzimu wa Yehova, iye naweruza Israele, natuluka kunkhondo; napereka Yehova Kusani-Risataimu mfumu ya Mesopotamiya m’dzanja lake; ndi dzanja lake linamgonjetsa Kusani-Risataimu.

11 Pamenepo dziko linapumula zaka makumi anai; ndi Otiniyele mwana wa Kenazi anafa.

Ehudi awalanditsa m’dzanja la Egiloni

12 Koma ana a Israele anaonjezanso kuchita choipa pamaso pa Yehova; pamenepo Yehova analimbitsa Egiloni mfumu ya Mowabu pa Israele, popeza anachita choipa pamaso pa Yehova.

13 Ndipo anadzisonkhanitsira ana a Amoni ndi a Amaleke, namuka nakantha Israele, nalanda mzinda wa m’migwalangwa nakhalamo.

14 Ndipo ana a Israele anatumikira Egiloni mfumu ya Mowabu zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu.

15 Koma pamene ana a Israele anafuula kwa Yehova, Yehova anawaukitsira mpulumutsi, Ehudi mwana wa Gera, Mbenjamini, munthu wamanzere, ndipo ana a Israele anatumiza mtulo m’dzanja lake kwa Egiloni mfumu ya Mowabu.

16 Ndipo Ehudi anadzisulira lupanga lakuthwa konsekonse utali wake mkono; nalimangirira pansi pa zovala zake pa ntchafu ya kulamanja.

17 Ndipo anapereka mtulo kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu; koma Egiloni ndiye munthu wonenepa ndithu.

18 Ndipo atatha kupereka mtulowo, anauza anthu onyamula mtulo achoke.

19 Koma iye mwini anabwerera pa mafano osema ali ku Giligala, nati, Ndili nao mau achinsinsi kwa inu, mfumu. Nati iye, Khalani chete. Ndipo anatuluka onse akuimapo.

20 Ndipo Ehudi anamdzera alikukhala pa yekha m’chipinda chosanja chopitidwa mphepo. Nati Ehudi, Ndili nao mau a Mulungu akukuuzani. Nauka iye pa mpando wake.

21 Ndipo Ehudi anatulutsa dzanja lake lamanzere nagwira lupanga ku ntchafu ya kulamanja nampyoza m’mimba mwake;

22 ndi chigumbu chake chinalowa kutsata mpeni wake; ndi mafuta anaphimba mpeniwo, pakuti sanasolole lupanga m’mimba mwake; nilituluka kumbuyo.

23 Pamenepo Ehudi anatuluka kukhonde namtsekera pamakomo pa chipinda chosanja nafungulira.

24 Ndipo atatuluka iye, anadza akapolo ake; napenya, ndipo taonani pamakomo pa chipinda chosanja mpofungulira; nati iwo, Angophimba mapazi m’chipinda chake chosanja chopitidwa mphepo.

25 Ndipo analindirira mpaka anachita manyazi; koma taonani, sanatsegule pamakomo pa chipinda chosanja. Pamenepo anatenga mfungulo natsegula; ndipo taonani, mbuye wao wagwa pansi, wafa.

26 Ndipo Ehudi anapulumuka pakuchedwa iwo, napitirira pa mafano osema, napulumuka kufikira Seira.

27 Ndipo kunali, pakufika iye anaomba lipenga ku mapiri a Efuremu; ndi ana a Israele anatsika naye kuchokera kumapiri, nawatsogolera iye.

28 Ndipo ananena nao, Nditsateni ine, pakuti Yehova wapereka adani anu Amowabu m’manja mwanu. Ndipo anatsika ndi kumtsata, natsekereza Amowabu madooko a Yordani, osalola mmodzi aoloke.

29 Ndipo anakantha Amowabu nyengo ija anthu zikwi khumi, onsewa anthu amoyo, ndi ngwazi; ndipo sanapulumuke ndi mmodzi yense.

30 Motero anagonjetsa Mowabu tsiku lija pansi padzanja la Israele. Ndipo dziko linapumula zaka makumi asanu ndi atatu.

31 Atapita iye kunali Samigara, mwana wa Anati amene anakantha Afilisti mazana asanu ndi limodzi ndi mtoso wa ng’ombe; nayenso anapulumutsa Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/3-60ebbecb9e2f6fe0959ab541362c07a2.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 4

Debora ndi Baraki alanditsa Aisraele m’dzanja la Yabini

1 Ndipo ana a Israele anaonjeza kuchita choipa pamaso pa Yehova, atafa Ehudi.

2 Ndipo Yehova anawagulitsa m’dzanja la Yabini mfumu ya Kanani, wochita ufumu ku Hazori; kazembe wake wa nkhondo ndiye Sisera, wokhala ku Haroseti waamitundu.

3 Ndipo ana a Israele anafuula kwa Yehova; pakuti anali nao magaleta achitsulo mazana asanu ndi anai; napsinja ana a Israele kolimba zaka makumi awiri.

4 Ndipo Debora,mneneriwamkazi, ndiye mkazi wake wa Lapidoti, anaweruza Israele nyengo ija.

5 Ndipo anakhala patsinde pa mgwalangwa wa Debora pakati pa Rama ndi Betele ku mapiri a Efuremu; ndi ana a Israele anakwera kwa iye awaweruze.

6 Ndipo anatuma, naitana Baraki mwana wa Abinowamu, achoke mu Kedesi-Nafutali; nanena naye, Kodi Yehova Mulungu wa Israele sanalamulire ndi kuti, Muka, nulunjike kuphiri la Tabori, nuwatenge, apite nawe anthu zikwi khumi a ana a Nafutali ndi ana a Zebuloni?

7 Ndipo ndidzamkoka Sisera, kazembe wa nkhondo ya Yabini, akudzere ku mtsinje wa Kisoni, ndi magaleta ake, ndi aunyinji ake; ndipo ndidzampereka m’dzanja lako.

8 Ndipo Baraki anati kwa iye, Ukamuka nane, ndidzamuka; ukapanda kumuka nane, sindimuka.

9 Nati iye, Kumuka ndidzamuka nawe, koma ulendo umukawo, sudzachita nao ulemu; pakuti Yehova adzagulitsa Sisera m’dzanja la mkazi. Motero Debora anauka namuka ndi Baraki ku Kedesi.

10 Ndipo Baraki anaitana Zebuloni ndi Nafutali asonkhane ku Kedesi; iye nakwera ndi anthu zikwi khumi akumtsata; Deboranso anakwera kunka naye.

11 Ndipo Hebere Mkeni anadzisiyanitsa ndi Akeni, ndi ana a Hobabu mlamu wake wa Mose, namanga mahema ake mpaka thundu wa mu Zaananimu, ndiwo wa ku Kedesi.

12 Ndipo anauza Sisera kuti Baraki mwana wa Abinowamu wakwera kuphiri la Tabori.

13 Pamenepo Sisera anasonkhanitsa magaleta ake onse ndiwo magaleta mazana asanu ndi anai achitsulo, ndi anthu onse okhala naye, kuyambira Haroseti wa amitundu mpaka mtsinje wa Kisoni.

14 Ndipo Debora anati kwa Baraki, Nyamuka; pakuti ili ndi tsikuli Yehova wapereka Sisera m’dzanja lako; sanatuluke kodi Yehova pamaso pako? Potero Baraki anatsika kuphiri la Tabori ndi amuna zikwi khumi akumtsata.

15 Ndipo Yehova anaononga Sisera ndi magaleta onse ndi gulu lankhondo lonse, ndi lupanga lakuthwa pamaso pa Baraki; koma Sisera anatsika pagaleta nathawa choyenda pansi.

16 Koma Baraki anatsata magaleta ndi gululo mpaka Haroseti wa amitundu; ndi gulu lonse lankhondo la Sisera linagwa ndi lupanga lakuthwa, sanatsale munthu ndi mmodzi yense.

17 Koma Sisera anathawira choyenda pansi ku hema wa Yaele mkazi wa Hebere Mkeni; pakuti panali mtendere pakati pa Yabini mfumu ya Hazori, ndi nyumba ya Hebere Mkeni.

18 Ndipo Yaele anatuluka kukomana ndi Sisera, nanena naye, Patuka, mbuye wanga, patukira kwa ine kuno; usaope. Ndipo anapatukira kwa iye kulowa m’hema, namfunda ndi chimbwi.

19 Pamenepo ananena naye, Ndipatsetu madzi pang’ono ndimwe; popeza ndine waludzu. Ndipo anatsegula thumba la mkaka, nampatsa amwe, namfunda.

20 Ndipo Sisera ananena naye, Taima pakhomo pa hema, ndipo kudzali, akadza munthu, akakufunsa akati, Pali munthu pano kodi? Uziti, Palibe.

21 Pamenepo Yaele mkazi wa Hebere anatenga chichiri cha hema, natenga nyundo m’dzanja lake namdzera monyang’ama, nakhomera chichiri chilowe m’litsipa mwake; ndipo chinapyoza kulowa m’nthaka; popeza anali m’tulo tofa nato ndi kulema; nafa.

22 Ndipo taonani, pomlondola Sisera Barakiyo, Yaele anatuluka kukomana naye, nati kwa iye, Idza kuno, ndidzakuonetsa munthu umfunayo. Potero anamdzera, ndipo taonani, Sisera wagwa, wafa, ndi chichiri m’litsipa mwake.

23 Momwemo Mulungu anagonjetsa tsiku lija Yabini mfumu ya Kanani pamaso pa ana a Israele.

24 Ndipo dzanja la ana a Israele linankabe ndi kulimbika pa Yabini mfumu ya Kanani mpaka adamuononga Yabini mfumu ya Kanani.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/4-6c3dd0c90a55cbda0d7382cc4f081d51.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 5

Nyimbo ya Debora

1 Ndipo Debora ndi Baraki mwana wa Abinowamu anaimba tsiku lomwelo ndi kuti,

2 Lemekezani Yehova

pakuti atsogoleri mu Israele anatsogolera,

pakuti anthu anadzipereka mwaufulu.

3 Imvani mafumu inu; tcherani makutu, akalonga inu;

ndidzamuimbira ine Yehova, inetu;

ndidzamuimbira nyimbo, Yehova, Mulungu wa Israele.

4 Yehova, muja mudatuluka mu Seiri,

muja mudayenda kuchokera ku thengo la Edomu,

dziko linanjenjemera, thambo lomwe linakha,

inde mitambo inakha madzi.

5 Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,

Sinai lili pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israele.

6 Masiku a Samigara, mwana wa Anati,

masiku a Yaele maulendo adalekeka

ndi apanjira anayenda mopazapaza.

7 Midzi idalekeka mu Israele, idalekeka.

Mpaka ndinauka ine Debora,

ndinauka ine amai wa Israele.

8 Anasankha milungu yatsopano,

pamenepo nkhondo inaoneka kuzipata.

Ngati chikopa kapena nthungo zidaoneka

mwa zikwi makumi anai a Israele?

9 Mtima wanga uvomerezana nao olamulira a mu Israele,

amene anadzipereka mwaufulu mwa anthu.

Lemekezani Yehova.

10 Inu akuyenda okwera pa abulu oyera,

inu akukhala poweruzira,

ndi inu akuyenda m’njira, fotokozerani.

11 Posamveka phokoso la amauta potunga madzi,

pomwepo adzafotokozera zolungama anazichita Yehova,

zolungama anazichita m’madera ake, mu Israele.

Pamenepo anthu a Yehova anatsikira kuzipata.

12 Galamuka, Debora, galamuka,

galamuka, galamuka, unene nyimbo;

uka, Baraki, manga nsinga ndende zako, mwana wa Abinowamu, iwe.

13 Pamenepo omveka otsala anatsika ndi anthu;

Yehova ananditsikira pakati pa achamuna.

14 Anafika Aefuremu amene adika mizu mu Amaleke;

Benjamini anakutsata iwe pakati pa anthu ako.

Ku Makiri kudachokera olamulira,

ndi ku Zebuloni iwo akutenga ndodo ya mtsogoleri.

15 Akalonga a Isakara anali ndi Debora;

monga Isakara momwemo Baraki,

anawatuma m’chigwa nanka choyenda pansi.

Pa mitsinje ya Rubeni panali zotsimikiza mtima zazikulu.

16 Wakhaliranji pakati pa makola,

kumvera kulira kwa zoweta?

Ku timitsinje ta Rubeni kunali zotsimikiza mtima zazikulu.

17 Giliyadi anakhala tsidya lija la Yordani;

ndi Dani, akhaliranji m’zombo?

Asere anakhala pansi m’mphepete mwa nyanja,

nakhalitsa pa nyondo yake ya nyanja.

18 Zebuloni ndiwo anthu anataya moyo wao mpaka imfa,

Nafutali yemwe poponyana pamisanje.

19 Anadza mafumu nathira nkhondo;

pamenepo anathira nkhondo mafumu a Kanani.

Mu Taanaki, ku madzi a Megido;

osatengako phindu la ndalama.

20 Nyenyezi zinathira nkhondo yochokera kumwamba,

m’mipita mwao zinathirana ndi Sisera.

21 Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,

mtsinje uja wakale, mtsinje wa Kisoni.

Yenda mwamphamvu, moyo wangawe.

22 Pamenepo ziboda za akavalo zinaguguda.

Ndi kutumphatumpha, kutumphatumpha kwa anthu ake eni mphamvu.

23 Mutemberere Merozi, ati mthenga wa Yehova,

mutemberere chitemberere nzika zake;

pakuti sanadzathandize Yehova,

kumthandiza Yehova pa achamuna.

24 Wodalitsika, woposa akazi, akhale Yaele

mkazi wa Hebere Mkeni.

Akhale wodalitsika woposa akazi a m’hema.

25 Mwamunayo anapempha madzi, anampatsa mkaka,

anamtengera mafuta a mkaka m’chotengera cha mfulu.

26 Dzanja lake analitambasulira kuchichiri,

ndi dzanja lake lamanja ku nyundo ya antchito,

nakhomera Sisera, nakantha mutu wake,

inde, anaphwanya napyoza m’litsipa mwake.

27 Pa mapazi ake anabzong’onyoka, anagwa, anagona;

pa mapazi ake anabzong’onyoka, anagwa;

pobzong’onyokapo, pamenepo wagwa wafa.

28 Anapenyerera ali pazenera,

nafuula Make wa Sisera, pa sefa wake,

achedweranji galeta wake?

Zizengerezeranji njinga za magaleta ake?

29 Akazi anzake omveka anzeru anamyankha;

koma anadziyankhira yekha mau.

30 Kodi sanapeze, sanagawe zofunkha?

Namwali, anamwali awiri kwa munthu aliyense.

Chofunkha cha nsalu za mawangamawanga kwa Sisera;

chofunkha cha nsalu za mawangamawanga, za maluwa,

nsalu za mawangamawanga, za maluwa konsekonse,

kwa chofunkha cha khosi lake.

31 Adani anu onse, Yehova, atayike momwemo.

Koma iwo akukonda Inu

akhale ngati dzuwa lotuluka mu mphamvu yake.

Ndipo dziko linapumula zaka makumi anai.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/5-b7c4b6c396c76e3cf64902a6c6e904a8.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 6

Midiyani agonjetsa Aisraele

1 Koma ana a Israele anachita choipa pamaso pa Yehova; ndipo Yehova anawapereka m’dzanja la Midiyani zaka zisanu ndi ziwiri.

2 Pamene dzanja la Midiyani linagonjetsa Israele, ana a Israele anadzikonzera ming’ang’ala ya m’mapiri, ndi mapanga, ndi malinga chifukwa cha Midiyani.

3 Ndipo kunali, akabzala Israele, amakwera Amidiyani, ndi Amaleke, ndi ana a kum’mawa, inde amawakwerera;

4 nawamangira misasa, namaononga zipatso za m’dziko mpaka ufika ku Gaza, osawasiyira chochirira njala mu Israele, ngakhale nkhosa, kapena ng’ombe, kapena bulu.

5 Pakuti anakwera nazo zoweta zao ndi mahema ao, analowa ngati dzombe kuchuluka kwao; iwowa ndingamirazao zomwe nzosawerengeka; ndipo analowa m’dziko kuliononga.

6 Ndipo Israele anafooka kwambiri chifukwa cha Midiyani; ndipo ana a Israele anafuula kwa Yehova.

7 Ndipo kunali, pamene ana a Israele anafuula kwa Yehova chifukwa cha Midiyani,

8 Yehova anatuma munthumnenerikwa ana a Israele, nanena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israele, Ine ndinakukwezani kuchokera mu Ejipito, ndi kukutulutsani m’nyumba ya ukapolo;

9 ndipo ndinakulanditsani m’dzanja la Aejipito, ndi m’dzanja la onse akupsinja inu, ndi kuwaingitsa pamaso panu, ndi kukupatsani dziko lao;

10 ndipo ndinati kwa inu, Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musamaopa milungu ya Aamori amene mukhala m’dziko lao; koma simunamvere mau anga.

Mngelo wa Mulungu amdzera Gideoni

11 Pamenepo anadza mthenga wa Yehova, nakhala patsinde pa thundu wokhala mu Ofura, wa Yowasi Mwabiyezere; ndi mwana wake Gideoni analikuomba tirigu m’mopondera mphesa, awabisire Amidiyani.

12 Ndipo mthenga wa Yehova anamuonekera, nati kwa iye, Yehova ali nawe, ngwazi iwe, wamphamvu iwe.

13 Ndipo Gideoni ananena naye, Mbuye wanga, ngati Yehova ali nafe chatigwera ife bwanji chonsechi? Ndipo zili kuti zodabwitsa zake zonse zimene makolo athu anatiwerengera, ndi kuti, Sanatikweze kodi Yehova kuchokera mu Ejipito? Koma tsopano Yehova watitaya natipereka m’dzanja la Midiyani.

14 Pamenepo Yehova anamtembenukira, nati, Muka nayo mphamvu yako iyi, nupulumutse Israele m’dzanja la Midiyani. Sindinakutume ndi Ine kodi?

15 Ndipo anati kwa Iye, Ha! Mbuye, ndidzapulumutsa Israele ndi chiyani? Taonani, banja langa lili loluluka mu Manase, ndipo ine ndine wamng’ono m’nyumba ya atate wanga.

16 Ndipo Yehova ananena naye, Popeza Ine ndidzakhala nawe udzakantha Amidiyani ngati munthu mmodzi.

17 Ndipo anati kwa Iye, Ngati mundikomera mtima mundionetse chizindikiro tsopano chakuti ndi Inu wakunena nane.

18 Musachoke pano, ndikupemphani, mpaka ndikudzerani ndi kutulutsa chopereka changa ndi kuchiika pamaso panu. Ndipo anati, Ndidzalinda mpaka ubwera.

19 Ndipo Gideoni analowa, nakonza kambuzi ndi mikate yopanda chotupitsa ya efa wa ufa; nyamayi anaiika m’lichero, ndi msuzi anauthira mumbale, natuluka nazo kwa Iye ali patsinde pa thundu, nazipereka.

20 Koma mthenga wa Mulungu ananena naye, Tenga nyamayi ndi mikate yopanda chotupitsa ndi kuziika pathanthwe pano ndi kutsanula msuzi. Ndipo anatero.

21 Pamenepo mthenga wa Yehova anatambasula nsonga ya ndodo inali m’dzanja lake, nakhudza nyamayi ndi mikate yopanda chotupitsa; ndipo unatuluka moto m’thanthwe nunyeketsa nyama ndi mikate yopanda chotupitsa; ndi mthenga wa Yehova anakanganuka pamaso pake.

22 Pamenepo Gideoni anaona kuti ndiye mthenga wa Yehova, nati Gideoni, Tsoka ine, Yehova Mulungu! Popeza ndaona mthenga wa Yehova maso ndi maso.

23 Ndipo Yehova anati kwa iye, Mtendere ukhale ndi iwe, usaope, sudzafa.

24 Pamenepo Gideoni anammangira Yehova guwa la nsembe pomwepo; nalitcha Yehova-ndiye-mtendere; likali mu Ofura wa Aabiyezere ndi pano pomwe.

Gideoni agamula guwa la nsembe la Baala

25 Ndipo kunali, usiku womwe uja Yehova ananena naye, Tenga ng’ombe ya atate wako, ndiyo ng’ombe yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri, nugamule guwa la nsembe laBaalandilo la atate wako, nulikhe chifanizo chili pomwepo;

26 numangire Yehova Mulungu wako guwa la nsembe pamwamba pa lingali, monga kuyenera; nutenge ng’ombe yachiwiriyo, nufukize nsembe yopsereza; nkhuni zake uyese chifanizo walikhacho.

27 Pamenepo Gideoni anatenga amuna khumi mwa anyamata ake, nachita monga Yehova adanena naye; ndipo kunali, popeza anaopa akunyumba ya atate wake, ndi amuna akumudziwo, sanachichite msana, koma usiku.

28 Ndipo pakuuka mamawa amuna akumudziwo, taonani, guwa la nsembe la Baala litagamuka, ndi chifanizo chinali pomwepo chitalikhidwa ndi ng’ombe yachiwiri yoperekedwa paguwa la nsembe adalimanga.

29 Nanenana wina ndi mnzake, Wachita ichi ndani? Ndipo atafunafuna nafunsafunsa, anati, Gideoni, mwana wa Yowasi wachita ichi.

30 Pamenepo amuna akumudziwo anati kwa Yowasi, Umtulutse mwana wako kuti afe; pakuti anagamula guwa la nsembe la Baala, pakutinso analikha chifanizo chinali pomwepo.

31 Koma Yowasi anati kwa onse akumuimirira, Kodi inu mumnenera Baala mlandu? Kapena kodi mudzampulumutsa iye? Iye amene amnenera mlandu aphedwe kukali m’mawa; akakhala mulungu adzinenere yekha mlandu, popeza wina wamgamulira guwa lake la nsembe.

32 Chifukwa chake anamutcha tsiku lija Yerubaala, ndi kuti, Amnenere mlandu Baala popeza anamgamulira guwa lake la nsembe.

33 Pamenepo Amidiyani onse ndi Aamaleke ndi ana a kum’mawa anasonkhana pamodzi naoloka, namanga misasa m’chigwa cha Yezireele.

34 Koma mzimu wa Yehova unavala Gideoni; naomba lipenga iye, ndi a banja la Abiyezere analalikidwa kumtsata iye.

35 Ndipo anatuma mithenga kwa Manase konse; ndi iwonso analalikidwa kumtsata iye; natuma mithenga kwa Asere, ndi kwa Zebuloni, ndi kwa Nafutali; iwo nadzakomana nao.

36 Ndipo Gideoni anati kwa Mulungu, Mukadzapulumutsa Israele ndi dzanja langa monga mwanena,

37 taonani, ndidzaika chikopa cha ubweya popunthira tirigu; pakakhala mame pachikopa pokha, ndi panthaka ponse pouma, pamenepo ndidzadziwa kuti mudzapulumutsa Israele ndi dzanja langa monga mwanena.

38 Ndipo kunatero; pakuti anauka mamawa, nafinya chikopacho, nakamula mame a pachikopa, madzi ake odzala mbale.

39 Ndipo Gideoni ananena ndi Mulungu, Mkwiyo wanu usandiyakire, ndinene kamodzi kokha: ndikuyeseni kamodzi kokha ndi chikopa; paume pachikopa pokha, ndi panthaka ponse pakhale mame.

40 Ndipo Mulungu anatero usiku uja; pakuti panauma pachikopa pokha, ndi panthaka ponse panali mame.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/6-afa12d2564e06808671f6e2a4c8f0504.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 7

Gideoni apirikitsa nkhondo ya Amidiyani

1 Pamenepo Yerubaala, ndiye Gideoni, ndi anthu onse okhala naye anauka mamawa, namanga misasa pa chitsime cha Harodi, ndi misasa ya Midiyani inali kumpoto kwao, paphiri la More m’chigwa.

2 Ndipo Yehova anati kwa Gideoni. Anthu ali ndi iwe andichulukira kuti ndipereke Midiyani m’dzanja lao; angadzitame Israele pa Ine, ndi kuti, Dzanja la ine mwini landipulumutsa.

3 Ndipo tsopano, kalalike m’makutu a anthu, ndi kuti, Aliyense wochita mantha, nanjenjemera, abwerere nachoke paphiri la Giliyadi. Ndipo anabwererako anthu zikwi makumi awiri mphambu ziwiri, natsalako zikwi khumi.

4 Ndipo Yehova ananena ndi Gideoni, Anthu akali ochuluka; tsikira nao kumadzi, ndipo ndidzakuyesera iwo komweko; ndipo kudzali kuti iye amene ndimnena kwa iwe, Uyo azimuka nawe, yemweyo azimuka nawe; koma aliyense ndimnena kwa iwe, Uyo asamuke nawe, yemweyo asamuke.

5 Ndipo anatsikira nao anthu kumadzi; ndipo Yehova anati kwa Gideoni, Aliyense akapiza madzi pa lilime lake, monga akhatira galu, ameneyo amuike pa yekha; momwemo aliyense agwada pakumwa.

6 Ndi kuwerenga kwa iwo akukhatira, ndi kuika dzanja lao kukamwa kwao, ndiko mazana atatu; koma ena onse anagwada pakumwa madzi.

7 Ndipo Yehova anati kwa Gideoni, Ndi anthu mazana atatu akukhatira ndidzakupulumutsani, ndi kupereka Amidiyani m’dzanja lako; koma amuke anthu awa onse, yense kumalo kwake.

8 Pamenepo anthu anatenga kamba m’dzanja lao, ndi malipenga ao; ndipo anauza amuna onse a Israele amuke, yense kuhema kwake; koma anaimika amuna mazana atatuwo; ndipo misasa ya Midiyani inali kunsi kwake m’chigwa.

9 Ndipo kunali usiku womwewo, kuti Yehova ananena naye, Tauka, tatsikira kumisasa; pakuti ndaipereka m’dzanja lako.

10 Koma ngati uopa kutsika, utsike naye Pura mnyamata wako kumisasa;

11 nudzamva zonena iwo; utatero manja ako adzalimbikitsidwa kutsikira kumisasa. Pamenepo anatsikira ndi Pura mnyamata wake ku chilekezero cha anthu azida a m’misasa.

12 Ndipo Amidiyani ndi Aamaleke ndi ana onse a kum’mawa ali gonere m’chigwa, kuchuluka kwao ngati dzombe; ndingamirazao zosawerengeka, kuchuluka kwao ngati mchenga wa m’mphepete mwa nyanja.

13 Ndipo pakufikako Gideoni, taonani, panali munthu analikufotokozera mnzake loto, nati, Taona, kulota ndinalota, ndipo tapenya, mtanda wa mkate wabarele unakunkhulirakunkhulira m’misasa ya Midiyani, nufika kuhema, numgunda nagwa, numpidigula kuti hema anakhala chigwere.

14 Ndipo mnzake anayankha nati, Ichi si china konse koma lupanga la Gideoni mwana wa Yowasi, munthu wa Israele; Mulungu wapereka Midiyani ndi a m’misasa onse m’dzanja lake.

15 Ndipo kunali, pakumva Gideoni kufotokozera kwa lotolo ndi tanthauzo lake, anadziwerama; nabwera ku misasa ya Israele nati, Taukani, pakuti Yehova wapereka a m’misasa a Midiyani m’dzanja lanu.

16 Ndipo anagawa amuna mazana atatu akhale magulu atatu, napatsa malipenga m’manja a iwo onse, ndi mbiya zopanda kanthu, ndi miuni m’kati mwa mbiyazo.

17 Ndipo ananena nao, Mundipenyerere ine, ndi kuchita momwemo; ndipo taonani, pakufika ine pa chilekezero cha misasa, kudzali, monga ndichita ine, momwemo muzichita inu.

18 Pamene ndiomba lipenga, ine ndi onse okhala nane, inunso muziomba lipenga pozungulira ponse pa misasa, ndi kunena kuti, Yehova ndi Gideoni.

19 Motero Gideoni ndi amuna zana anali naye anafikira ku chilekezero cha misasa poyambira ulonda wa pakati, atasintha alonda tsopano apa; ndipo anaomba malipenga, naphwanya mbiya zokhala m’manja mwao.

20 Ndi magulu atatuwo anaomba malipenga, naswa mbiyazo, nagwira miuni ndi dzanja lao lamanzere, ndi malipenga m’dzanja lao lamanja kuwaomba; ndipo anafuula, Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.

21 Ndipo anaima yense m’mbuto mwake pozungulira misasa; pamenepo anathamanga a m’misasa onse, nafuula, nathawa.

22 Ndipo mazana atatuwa anaomba malipenga, ndipo Yehova anakanthanitsa yense mnzake ndi lupanga m’misasa monse; ndi a m’misasa anathawa mpaka ku Betesita ku Zerera, mpaka ku malire a Abele-Mehola pa Tabati.

23 Pamenepo anthu a Israele analalikidwa kuchokera ku Nafutali, ndi ku Asere, ndi ku Manase yense, nalondola Amidiyani.

24 Gideoni anatumanso mithenga ku mapiri onse a Efuremu ndi kuti, Tsikani, kukomana ndi Amidiyani ndi kutsekereza madooko asanafike iwowa, mpaka ku Betebara ndi Yordani. Potero amuna onse a Efuremu anasonkhana pamodzi natsekereza madooko mpaka ku Betebara, ndi Yordani.

25 Ndipo anagwira akalonga awiri a Midiyani, Orebu ndi Zeebu; namupha Orebu ku thanthwe la Orebu; ndi Zeebu anamupha ku choponderamo mphesa cha Zeebu, nalondola Amidiyani; ndipo anadza nayo mitu ya Orebu ndi Zeebu kwa Gideoni tsidya lija la Yordani.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/7-17171600689ad907b37788d840bfdd1e.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 8

1 Ndipo amuna a Efuremu anati kwa iye, Ichi watichitira nchiyani, osatiitana popita iwe kulimbana ndi Amidiyani? Natsutsana naye kolimba.

2 Koma ananena nao, Ndachitanji tsopano monga inu? Kodi kukunkha mphesa kwa Efuremu sikuposa kutchera mphesa kwa Abiyezere?

3 Mulungu anapereka m’dzanja lanu akalonga a Midiyani, Orebu ndi Zeebu, ndipo ndinakhoza kuchitanji monga inu? Pamenepo mkwiyo wao unamlezera, atanena mau awa.

A ku Sukoti ndi a ku Penuwele anyoza Gideoni nalangidwa naye

4 Ndipo Gideoni anafika ku Yordani, naoloka, iye ndi amuna mazana atatu anali naye, ali otopa koma ali chilondolere.

5 Ndipo ananena kwa amuna a ku Sukoti, Mupatsetu anthu awa akunditsata mitanda yamkate; pakuti atopa, ndipo ndilikulondola Zeba ndi Zalimuna mafumu a Midiyani.

6 Koma akalonga a ku Sukoti anati, Kodi manja a Zeba ndi Zalimuna ali m’dzanja lako tsopano apa, kuti ife tiwaninkhe ankhondo ako mkate?

7 Ndipo Gideoni anati, Chifukwa chake, Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna m’dzanja langa, ndidzapuntha nyama yanu ndi minga ya m’chipululu ndi mitungwi.

8 Ndipo anachokapo kukwera ku Penuwele, nanena nao momwemo; ndipo amuna a ku Penuwele anamyankha monga adamyankha amuna a ku Sukoti.

9 Ndipo ananenanso kwa amuna a ku Penuwele ndi kuti, Ndikabwerera ndi mtendere ndidzagumula nsanja iyi.

10 Zeba ndi Zalimuna ndipo anali mu Karikori, ndi a m’misasa ao pamodzi nao, amuna monga zikwi khumi ndi zisanu; ndiwo otsala onse a khamu lonse la ana a kum’mawa; popeza atagwa amuna zikwi zana limodzi ndi makumi awiri akusolola lupanga.

11 Ndipo Gideoni anakwerera njira ya iwo okhala m’mahema kum’mawa kwa Noba, ndi Yogobeha, nakantha khamulo popeza khamulo linakhala lokhazikika mtima.

12 Ndipo Zeba ndi Zalimuna anathawa; koma anawatsata, nagwira mafumu awiri a Midiyani Zeba ndi Zalimuna, nanjenjemeretsa khamu lonse.

13 Pamenepo Gideoni mwana wa Yowasi anabwerera kunkhondo pokwerera pa Heresi.

14 Ndipo anagwira mnyamata wa anthu a ku Sukoti, nafunsira; ndipo anamsimbira akalonga a ku Sukoti, ndi akulu ake amuna makumi asanu ndi awiri kudza asanu ndi awiri.

15 Ndipo anafika kwa amuna a ku Sukoti, nati, Tapenyani Zeba ndi Zalimuna amene munanditonza nao ndi kuti, Kodi manja a Zeba ndi Zalimuna akhala m’dzanja lako, kuti tiwaninkhe mkate amuna ako akulema?

16 Ndipo anagwira akulu a m’mzinda ndi minga ya kuchipululu ndi mitungwi, nawalanga nazo amuna a ku Sukoti.

17 Ndipo anagamula nsanja ya Penuwele, napha amuna akumzinda.

18 Pamenepo anati kwa Zeba ndi Zalimuna, Amunawo munawapha ku Tabori anali otani? Iwo nayankha, Monga iwe momwemo iwowa; yense wakunga mwana wa mfumu.

19 Ndipo anati, Ndiwo abale anga, ana a mai wanga. Pali Yehova mukadawasunga amoyo, sindikadakuphani.

20 Nati kwa Yetere mwana wake woyamba, Tauka, nuwaphe. Koma mnyamatayo sanasolole lupanga lake; pakuti anaopa, pokhala anali mnyamata.

21 Pamenepo Zeba ndi Zalimuna anati, Tauka iwe mwini nutigwere; pakuti monga munthu momwemo mphamvu yake. Ndipo Gideoni anauka nawapha Zeba ndi Zalimuna, nalanda mphande zinali kukhosi kwangamirazao.

Gideoni akana kulowa ufumu

22 Pamenepo anthu a Israele anati kwa Gideoni, Mutilamulire ndi inu, ndi mwana wanu, ndi mdzukulu wanu, pakuti mwatipulumutsa m’dzanja la Amidiyani.

23 Koma Gideoni ananena nao. Sindidzalamulira inu, ngakhale mwana wanga sadzalamulira inu; Yehova adzalamulira inu.

24 Gideoni anatinso kwa iwo, Mundilole ndipemphe kanthu kamodzi kwa inu, mundipatse aliyense maperere mwa zofunkha zanu; pakuti anali nao maperere agolide, pokhala anali Aismaele.

25 Ndipo anayankha, Kupereka tiwapereka; nayalapo chovala, naponyamo yense maperere a mwa zofunkha zao.

26 Ndipo kulemera kwake kwa maperere agolide adawapempha ndiko masekeli chikwi chimodzi ndi mazana asanu ndi awiri; osawerenga mphande, ndi zitunga ndi zovala zachibakuwa za pa mafumu a ku Midiyani, osawerenganso maunyolo okhala pa makosi a ngamira zao.

27 Ndipo Gideoni anawapanga fano, naliika m’mzinda mwake, ndiwo Ofura; ndi Israele yense analitsata kuligwadira pomwepo; ndipo linakhala kwa Gideoni ndi nyumba yake ngati msampha.

28 Motero anagonjetsa Amidiyani pamaso pa ana a Israele, osaweramutsanso mitu yao iwowa. Ndipo dziko lidapumula zaka makumi anai m’masiku a Gideoni.

29 Ndipo Yerubaala, mwana wa Yowasi anamuka, nakhala m’nyumba ya iye yekha.

30 Nakhala nao ana aamuna makumi asanu ndi awiri Gideoni, anawabala ndi iye; popeza anali nao akazi ambiri.

31 Ndipo mkazi wake wamng’ono wokhala mu Sekemu, iyenso anambalira mwana wamwamuna; namutcha dzina lake Abimeleki.

32 Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi anafa atakalamba bwino, naikidwa m’manda a Yowasi atate wake, mu Ofura wa Aabiyezere.

33 Ndipo kunali, atafa Gideoni, ana a Israele anabwereranso nagwadira Abaala, nayesa Baala-Beriti mulungu wao.

34 Ndi ana a Israele sanakumbukire Yehova Mulungu wao, amene anawapulumutsa m’dzanja la adani ao onse pozungulira ponse;

35 osachitira chifundo nyumba ya Yerubaala, ndiye Gideoni, monga mwa zokoma zonse iye anachitira Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/8-a6be2e9727e28464d018e0d24de7334e.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 9

Abimeleki awapha abale ake

1 Koma Abimeleki mwana wa Yerubaala anamuka ku Sekemu kwa abale a amai wake, nanena nao, ndi kwa banja lonse la nyumba ya atate wa amai wake, ndi kuti,

2 Nenanitu m’makutu mwa eni ake onse a ku Sekemu, Chokomera inu nchiti, akulamulireni ana aamuna onse a Yerubaala ndiwo amuna makumi asanu ndi awiri, kapena akulamulireni mwamuna mmodzi? Mukumbukirenso kuti ine ndine wa fuko lanu ndi nyama yanu.

3 Pamenepo abale a amake anamnenera mau awa onse m’makutu a eni ake onse a Sekemu; ndi mitima yao inalunjika kutsata Abimeleki; pakuti anati, Ndiye mbale wathu.

4 Ndipo anampatsa ndalama makumi asanu ndi awiri za m’nyumba ya Baala-Beriti; ndipo Abimeleki analembera nazo anthu opanda pake ndi opepuka amene anamtsata.

5 Ndipo anamuka kunyumba ya atate wake ku Ofura, nawapha abale ake ana a Yerubaala, ndiwo amuna makumi asanu ndi awiri, pa thanthwe limodzi; koma Yotamu mwana wamng’ono wa Yerubaala anatsalako; pakuti anabisala.

6 Pamenepo anasonkhana eni ake onse a ku Sekemu, ndi nyumba yonse ya Milo, namuka namlonga Abimeleki ufumu pa thundu wa choimiritsa chili mu Sekemu.

Fanizo la Yotamu

7 Ndipo atamuuza Yotamu, anamuka iye naimirira pamutu paphiri la Gerizimu, nakweza mau ake, nafuula, nanena nao, Mundimvere ine, eni ake a ku Sekemu inu, kuti Mulungu amvere inu.

8 Kumuka inamuka mitengo kudzidzozera mfumu; niti kwa mtengo waazitona, Ukhale iwe mfumu yathu.

9 Koma mtengo wa azitona unati kwa iwo, Ngati ndidzasiya kunona kwanga kumene alemekeza nako Mulungu ndi anthu kukalenga pa mitengo?

10 Pamenepo mitengo inati kwa mkuyu. Tiye iwe, ukhale mfumu yathu.

11 Koma mkuyu unanena nao, Ngati ndidzasiya kuzuna kwanga, ndi zipatso zanga zokoma kukalenga pa mitengo?

12 Pamenepo mitengo inati kwa mpesa, Tiye iwe, ukhale mfumu yathu.

13 Koma mpesa unanena nao, Ngati ndidzasiya vinyo wanga wakusekeretsa Mulungu ndi anthu, kukalenga pa mitengo?

14 Pamenepo mitengo yonse inati kwa nkandankhuku, Tiye iwe, ukhale mfumu yathu.

15 Ndipo nkandankhuku unati kwa mitengo, Mukandidzoza mfumu yanu moonadi, tiyeni, thawirani ku mthunzi wanga; mukapanda kutero utuluke moto m’nkandankhuku ndi kunyeketsa mikungudza ya Lebanoni.

16 Ndipo tsopano, ngati mwachita moona ndi mwangwiro pakulonga Abimeleki ufumu, ngatinso mwamchitira chokoma Yerubaala ndi nyumba yake, ndi kumchitira monga anayenera manja ake;

17 pakuti atate wanga anakugwirirani nkhondo, nataya moyo wake, nakupulumutsani m’dzanja la Amidiyani;

18 koma mwaukira nyumba ya atate wanga lero lino, ndi kuwapha ana ake, ndiwo amuna makumi asanu ndi awiri, pa thanthwe limodzi; ndipo mwalonga Abimeleki mwana wa mdzakazi wake, akhale mfumu ya pa eni ake a ku Sekemu, chifukwa ali mbale wanu;

19 ngati tsono mwachitira Yerubaala ndi nyumba yake zoona ndi zangwiro lero lino, kondwerani naye Abimeleki, nayenso akondwere nanu;

20 koma ngati simunatero, utuluke moto kwa Abimeleki, nunyeketse eni ake a ku Sekemu ndi nyumba ya Milo; nutuluke moto kwa eni ake a ku Sekemu, ndi kunyumba yake ya Milo, nunyeketse Abimeleki.

21 Pamenepo Yotamu anafulumira, nathawa, namuka ku Beere, nakhala komweko, chifukwa cha Abimeleki mbale wake.

Mpanduko wa Gaala

22 Abimeleki atakhala kalonga wa Israele zaka zitatu,

23 Mulungu anatumiza mzimu woipa pakati pa Abimeleki ndi eni ake a ku Sekemu; ndi eni ake a ku Sekemu anamchitira Abimeleki mosakhulupirika;

24 kuti chiwawa adachitira ana aamuna makumi asanu ndi awiri a Yerubaala chimdzere, ndi kuti mwazi wao uikidwe pa mbale wao Abimeleki anawaphayo, ndi pa eni ake a ku Sekemu, amene analimbikitsa manja ake, awaphe abale ake.

25 Ndipo eni ake a ku Sekemu anaika omlalira pamwamba pa mapiri; amene anawawanya onse akudzera njirayi; ndipo anamuuza Abimeleki.

26 Ndipo Gaala, mwana wa Ebedi anadza ndi abale ake, napita ku Sekemu; ndi eni ake a ku Sekemu anamkhulupirira.

27 Ndipo anatuluka kunka kuminda, natchera mphesa m’mindamo, naponda mphesa, napereka nsembe yolemekeza, nalowa m’nyumba ya mulungu wao, nadya, namwa, natemberera Abimeleki.

28 Pamenepo Gaala, mwana wa Ebedi anati, Abimeleki ndani, ndi Sekemu ndani, kuti timtumikire? Sindiye mwana wa Yerubaala kodi? Ndi Zebuli kazembe wake? Mutumikire amuna a Hamori atate wa Sekemu; koma ameneyo timtumikire chifukwa ninji?

29 Mwenzi anthu awa akadakhala m’dzanja langa; ndikadamchotsadi Abimeleki. Ndipo anati kwa Abimeleki, Chulukitsa khamu lako, nutuluke.

30 Pamene Zebuli woyang’anira mzinda anamva mau a Gaala mwana wa Ebedi, anapsa mtima.

31 Natuma mithenga kwa Abimeleki ku Aruma monyenga nati, Taonani Gaala mwana wa Ebedi ndi abale ake afika ku Sekemu; ndipo taonani, akupandukitsirani mzinda.

32 Ndipo tsopano, taukani usiku, inu ndi anthu okhala nanu ndi kulalira kuthengo;

33 ndipo kukhale kuti m’mawa, pakutuluka dzuwa, muuke mamawa mugwere mzindawo; ndipo taonani, akakutulukirani iye ndi anthu ali naye, uzimchitira monga lidziwa dzanja lako.

34 Pamenepo Abimeleki anauka ndi anthu onse anali naye, usiku; nalalira a ku Sekemu, magulu anai.

35 Ndipo Gaala mwana wa Ebedi anatuluka, naima polowera pa chipata cha mzinda; naika Abimeleki ndi anthu anali naye m’molalira.

36 Ndipo pamene Gaala anapenya anthuwo anati kwa Zebuli, Taona, alikutsika anthu kuchokera pamwamba pa mapiri. Koma Zebuli ananena naye, Uona mthunzi wa mapiri ndi kuyesa anthu.

37 Koma Gaala ananenanso, nati, Tapenya alikutsika anthu pakati padziko, ndi gulu limodzi lidzera njira ya ku thundu wa alauli.

38 Pamenepo Zebuli anati kwa iye, Pakamwa pako mpoti tsopano, muja udanena, Ndani Abimeleki kuti timtumikire? Awa si anthuwo unawapeputsa? Utuluke tsopano, nulimbane nao.

39 Ndipo Gaala anatuluka pamaso pao pa eni ake a ku Sekemu, nalimbana ndi Abimeleki.

40 Koma Abimeleki anampirikitsa, nathawa iye pamaso pake; nagwa olasidwa ambiri mpaka polowera pa chipata.

41 Ndipo Abimeleki anakhala ku Aruma; ndi Zebuli anaingitsa Gaala ndi abale ake kuti asakhale mu Sekemu.

42 Ndipo kunali m’mawa mwake, kuti anthu anatuluka kunka kuminda; ndipo anauza Abimeleki.

43 Pamenepo anatenga anthu, nawagawa magulu atatu, nalalira m’minda; napenya, ndipo taonani, anthu alimkutuluka m’mzinda; nawaukira iye nawakantha.

44 Ndi Abimeleki ndi magulu okhala naye anathamanga naima polowera pa chipata cha mzinda; ndi magulu awiriwo anagwera onse okhala m’munda, nawakantha.

45 Ndipo Abimeleki analimbana ndi mzinda tsiku lija lonse; nalanda mzinda nawapha anthu anali m’mwemo; napasula mzinda; nawazapo mchere.

46 Ndipo pamene eni ake onse a Nsanja ya ku Sekemu anachimva, analowa m’ngaka ya nyumba ya Eliberiti.

47 Ndipo anauza Abimeleki kuti amuna onse a Nsanja ya ku Sekemu asonkhana.

48 Pamenepo Abimeleki anakwera kunka kuphiri la Zalimoni, iye ndi anthu onse anali naye; natenga nkhwangwa m’dzanja lake Abimeleki, nadula nthambi kumitengo, nainyamula ndi kuiika paphewa pake, nati kwa anthu okhala naye, Ichi munachiona ndachita, fulumirani, muchite momwemo.

49 Ndi anthu onse anadulanso yense nthambi yake, natsata Abimeleki, naziika pangaka, natentha nazo ngakayo ndi moto; motero anthu onse a Nsanja ya ku Sekemu anafanso, amuna ndi akazi ngati chikwi chimodzi.

Imfa ya Abimeleki

50 Pamenepo Abimeleki anamuka ku Tebezi, naumangira Tebezi misasa, naulanda.

51 Koma m’mzindamo munali nsanja yolimba nathawira kumeneko amuna ndi akazi onse, ndi eni ake onse a mzindawo, nadzitsekereza m’mwemo, nakwera patsindwi pa nsanja.

52 Ndipo Abimeleki anafika kunsanja, nalimbana nayo nkhondo, nayandikira kukhomo kwa nsanja, aitenthe ndi moto.

53 Ndipo mkazi wina anaponya mwala wa mphero pamutu pa Abimeleki, naphwanya bade lake.

54 Pamenepo anaitana msanga mnyamata wake wosenza zida zake, nanena naye, Solola lupanga lako nundiphe, angamanenere anthu, ndi kuti, Anamupha ndi mkazi. Nampyoza mnyamata wake, nafa iye.

55 Pamene amuna a Israele anaona kuti adafa Abimeleki anamuka yense kumalo kwake.

56 Momwemo Mulungu anambwezera Abimeleki choipacho anachitira atate wake ndi kuwapha abale ake makumi asanu ndi awiri.

57 Ndipo Mulungu anawabwezera choipa chonse cha amuna a ku Sekemu pamitu pao, ndipo linawagwera temberero la Yotamu mwana wa Yerubaala.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/9-3a3ca7324ffff31ab209fdb44f2633d1.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 10

Tola ndi Yairi aweruza Israele

1 Atafa Abimeleki, anauka kupulumutsa Israele Tola mwana wa Puwa, mwana wa Dodo munthu wa Isakara; nakhala iye mu Samiri ku mapiri a Efuremu.

2 Ndipo anaweruza Israele zaka makumi awiri ndi zitatu, nafa, naikidwa mu Samiri.

3 Atafa iye, anauka Yairi Mgiliyadi, naweruza Israele zaka makumi awiri mphambu ziwiri.

4 Ndipo anali nao ana aamuna makumi atatu okwera pa ana a abulu makumi atatu, iwo ndipo anali nayo mizinda makumi atatu, otchedwa midzi ya Yairi, mpaka lero lino, ndiyo m’dziko la Giliyadi.

5 Nafa Yairi, naikidwa mu Kamoni.

Aisraele achimwira Mulungu nagonjetsedwa ndi Afilisti ndi Amoni

6 Ndipo ana a Israele anaonjeza kuchita choipa pamaso pa Yehova, natumikira Abaala, ndi Aasitaroti, ndi milungu ya Aramu, ndi milungu ya Sidoni, ndi milungu ya Mowabu, ndi milungu ya ana a Amoni, ndi milungu ya Afilisti; ndipo anamleka Yehova osamtumikira.

7 Pamenepo mkwiyo wa Yehova unayakira Israele, nawagulitsa m’dzanja la Afilisti, ndi m’dzanja la ana a Amoni.

8 Ndipo anaphwanya napsinja ana a Israele chaka chija, natero ndi ana onse a Israele okhala tsidya lija la Yordani m’dziko la Aamori, ndilo Giliyadi, zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu.

9 Ndipo ana a Amoni anaoloka Yordani kuthiranso nkhondo Yuda ndi Benjamini, ndi nyumba ya Efuremu; napsinjika kwambiri Israele.

10 Ndipo ana a Israele anafuula kwa Yehova ndi kuti, Takuchimwirani, popeza tasiya Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.

11 Ndipo Yehova anati kwa ana a Israele, Kodi sindinakupulumutsani kwa Aejipito ndi kwa Aamori, ndi kwa ana a Amoni, ndi kwa Afilisti?

12 Asidoni omwe, ndi Aamaleke, ndi Amaoni anakupsinjani. Pamenepo munafuula kwa Ine, ndipo ndinakupulumutsani m’dzanja lao.

13 Koma mwandisiya Ine ndi kutumikira milungu ina, chifukwa chake sindikupulumutsaninso.

14 Mukani ndi kufuulira kwa milungu munaisankha, ikupulumutseni nyengo ya kusauka kwanu.

15 Koma ana a Israele anati kwa Yehova, Tachimwa, mutichitire monga mwa zonse zikomera pamaso panu; komatu mutipulumutse lero lino, tikupemphani.

16 Pamenepo anachotsa milungu yachilendo pakati pao, natumikira Yehova; ndipo mtima wake unagwidwa chisoni chifukwa cha mavuto a Israele.

17 Ndipo ana a Amoni analalikiridwa, namanga misasa mu Giliyadi. Ndi ana a Israele anasonkhana namanga misasa ku Mizipa.

18 Ndipo anthu, akalonga a Giliyadi, ananenana wina ndi mnzake, Ndaniyo adzayamba kulimbana ndi ana a Amoni? Iye adzakhala mkulu wa onse okhala mu Giliyadi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/10-ad807ccb666eb2a5e36efb3d611467f0.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 11

Yefita alanditsa Israele

1 Yefita Mgiliyadi ndipo anali ngwazi yamphamvu, ndiye mwana wa mkazi wadama; koma Giliyadi adabala Yefita.

2 Ndipo mkazi wa Giliyadi anambalira ana aamuna; koma atakula ana aamuna a mkaziyo anampirikitsa Yefita, nanena naye, Sudzalandira cholowa m’nyumba ya atate wako; pakuti ndiwe mwana wa mkazi wina.

3 Pamenepo Yefita anathawa abale ake, nakhala m’dziko la Tobu; ndipo anyamata opanda pake anasonkhana kwa Yefita, natuluka naye pamodzi.

4 Ndipo kunali, atapita masiku, ana a Amoni anachita nkhondo ndi Israele,

5 ndipo kunatero, pamene ana a Amoni anathira nkhondo pa Israele, akulu a Giliyadi anamuka kutenga Yefita m’dziko la Tobu;

6 nati kwa Yefita, Tiye ukhale kazembe wathu kuti tilimbane ndi ana a Amoni.

7 Ndipo Yefita anati kwa akulu a Giliyadi, Simunandide kodi, ndi kundichotsa m’nyumba ya atate wanga? Ndipo mundidzeranji tsopano pokhala muli m’kusauka?

8 Ndipo akulu a Giliyadi ananena ndi Yefita, Chifukwa chake chakuti takubwerera tsopano ndicho kuti umuke nafe ndi kuchita nkhondo ndi ana a Amoni, nudzakhala mkulu wathu wa pa onse okhala mu Giliyadi.

9 Ndipo Yefita anati kwa akulu a Giliyadi, Mukandifikitsanso kwathu kuchita nkhondo ndi ana a Amoni, nakawapereka Yehova pamaso panga, ndidzakhala mkulu wanu kodi?

10 Ndipo akulu a Giliyadi anati kwa Yefita, Yehova ndiye wakumvera pakati pa ife, tikapanda kuchita monga momwe wanena.

11 Pamenepo Yefita anamuka ndi akulu a Giliyadi, ndipo anthu anamuika mkulu wao ndi mtsogoleri wao; ndipo Yefita ananena mau ake onse pamaso pa Yehova ku Mizipa.

12 Ndipo Yefita anatuma mithenga kwa mfumu ya ana a Amoni, ndi kuti, Ndi chiyani ndi inu ndi kuti mwandidzera kuthira nkhondo dziko langa?

13 Ndipo mfumu ya ana a Amoni inati kwa mithenga ya Yefita, Chifukwa Israele analanda dziko langa pakukwera iye kuchokera ku Ejipito, kuyambira Arinoni mpaka Yaboki, ndi mpaka Yordani; ndipo tsopano undibwezere maikowa mwamtendere.

14 Ndipo Yefita anatumanso mithenga kwa mfumu ya ana a Amoni;

15 nanena naye, Atero Yefita, Israele sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la ana a Amoni;

16 pakuti pakukwera iwo kuchokera ku Ejipito Israele anayenda m’chipululu mpaka Nyanja Yofiira, nafika ku Kadesi;

17 pamenepo Israele anatuma mithenga kwa mfumu ya Edomu, ndi kuti, Ndikupemphani ndipitire pakati padziko lanu; koma mfumu ya Edomu siinamvera. Natumanso kwa mfumu ya Mowabu; nayenso osalola; ndipo Israele anakhala mu Kadesi.

18 Pamenepo anayenda m’chipululu, naphazira dziko la Edomu, ndi dziko la Mowabu, nadzera kum’mawa kwa dziko la Mowabu, namanga misasa tsidya lija la Arinoni; osalowa malire a Mowabu, pakuti Arinoni ndi malire a Mowabu.

19 Ndipo Israele anatuma mithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, mfumu ya ku Hesiboni; nanena naye Israele, Tikupemphani tipitire pakati padziko lanu, kunka kwathu.

20 Koma Sihoni sanakhulupirire Israele kuti apitire pakati pa malire ake; koma Sihoni anamemeza anthu ake onse, namanga misasa ku Yahazi, nathira nkhondo Israele.

21 Ndipo Yehova Mulungu wa Israele anapereka Sihoni ndi anthu ake onse m’dzanja la Israele, ndipo anawakantha, ndi Israele, analandira cholowa chake, dziko lonse la Aamori, nzika za m’dziko lija.

22 Ndipo analandira akhale cholowa chao, malire onse a Aamori, kuyambira Arinoni mpaka Yaboki, ndi kuyambira chipululu mpaka Yordani.

23 Motero Yehova Mulungu wa Israele anaingitsa Aamori, pamaso pa anthu ake Israele, ndipo kodi liyenera kukhala cholowa chanu?

24 Chimene akulandiritsani Kemosi mulungu wanu, simuchilandira cholowa chanu kodi? Momwemo aliyense Yehova Mulungu wathu waingitsa pamaso pathu, zakezo tilandira cholowa chathu.

25 Ndipo tsopano kodi inu ndinu wabwino woposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu; anatengana konse ndi Israele iyeyu kodi, kapena kuchita nao nkhondo konse kodi?

26 Pokhala Israele mu Hesiboni ndi midzi yake, ndi mu Aroere ndi midzi yake ndi m’mizinda yonse yokhala m’mphepete mwa Arinoni zaka mazana atatu; munalekeranji kulandanso nthawi ija?

27 Potero sindinakuchimwirani ine, koma mundichitira choipa ndinu kundithira nkhondo; Yehova Woweruzayo, aweruze lero lino pakati pa ana a Israele ndi ana a Amoni.

28 Koma mfumu ya ana a Amoni sanamvere mau a Yefita anamtumizirawo.

Chowinda cha Yefita

29 Pamenepo mzimu wa Yehova unamdzera Yefita, napitira iye ku Giliyadi, ndi Manase, napitira ku Mizipa wa Giliyadi, ndi kuchokera ku Mizipa wa Giliyadi anapitira kwa ana a Amoni.

30 Ndipo Yefita anawindira Yehova chowinda, nati, Mukaperekatu ana a Amoni m’dzanja langa,

31 ndipo kudzali kuti chilichonse chakutuluka pakhomo pa nyumba yanga kudzakomana nane pakubweranso ine ndi mtendere kuchokera kwa ana a Amoni, chidzakhala cha Yehova, ndipo ndidzachipereka nsembe yopsereza.

32 Potero Yefita anapita kwa ana a Amoni kuwathira nkhondo; ndipo Yehova anawapereka m’dzanja lake;

33 nawakantha kuyambira ku Aroere mpaka ufika ku Miniti, ndiyo mizinda makumi awiri, ndi ku Abele-Keranimu, makanthidwe aakulu ndithu. Motero ana a Amoni anagonjetsedwa pamaso pa ana a Israele.

34 Pofika Yefita ku Mizipa kunyumba yake, taonani, mwana wake wamkazi anatuluka kudzakomana naye ndi malingaka ndi kuthira mang’ombe; ndipo iyeyu anali mwana wake mmodzi yekha, analibe mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.

35 Ndipo kunali, pakumuona anang’amba zovala zake, nati, Tsoka ine, mwana wanga, wandiweramitsa kwakukulu, ndiwe wa iwo akundisaukitsa ine; pakuti ndamtsegulira Yehova pakamwa panga ine, ndipo sinditha kubwerera.

36 Ndipo anati kwa iye, Atate wanga, mwamtsegulira Yehova pakamwa panu, mundichitire ine monga umo mudatulutsa mau pakamwa panu; popeza Yehova anakuchitirani inu chilango pa adani anu, pa ana a Amoni.

37 Ndipo anati kwa atate wake, Andichitire ichi, andileke miyezi iwiri, kuti ndichoke ndi kutsikira kumapiri, ndi kulirira unamwali wanga, ine ndi anzanga.

38 Nati iye, Muka. Namuuza amuke akakhale miyezi iwiri; namuka iye ndi anzake, nalirira unamwali wake pamapiri.

39 Ndipo kunali pakutha miyezi iwiri, anabwerera kwa atate wake amene anamchitira monga mwa chowinda chake anachiwinda; ndipo sanamdziwe mwamuna. Motero unali mwambo mu Israele,

40 kuti ana aakazi a Israele akamuka chaka ndi chaka kumliririra mwana wa Yefita wa ku Giliyadi, masiku anai pa chaka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/11-23113561ae659784b23e39b308ae2a3c.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 12

Efuremu aukira Yefita

1 Pamenepo amuna a Efuremu analalikidwa, napita kumpoto; nati kwa Yefita, Wapitiriranji kuthira nkhondo ana a Amoni, osatiitana ife timuke nawe? Tidzakutenthera nyumba yako ndi moto pamutu pako.

2 Ndipo Yefita anati kwa iwo, Ine ndi anthu anga tinatsutsana kwakukulu ndi ana a Amoni, koma pamene ndinakuitanani inu simunandipulumutse m’dzanja lao.

3 Ndipo pakuona ine kuti simundipulumutsa, ndinataya moyo wanga ndi kupita kwa ana a Amoni; ndipo Yehova anawapereka m’dzanja langa; mwakwereranji tsono lero lino kundichitira nkhondo?

4 Pamenepo Yefita anamemeza amuna onse a mu Giliyadi nalimbana naye Efuremu; ndipo amuna a Giliyadi anakantha Efuremu, chifukwa adati, Inu Agiliyadi ndinu akuthawa Efuremu, pakati pa Efuremu ndi pakati pa Manase.

5 Ndipo Agiliyadi anatsekereza madooko a Yordani a Efuremu; ndipo kunatero kuti, akati othawa a Efuremu, Ndioloke, amuna a Giliyadi anati kwa Iye, Ndiwe Mwefuremu kodi? Akati, Iai;

6 pamenepo anati kwa iye, Unene tsono Shiboleti; ndipo akati, Siboleti, osakhoza kutchula bwino, amgwira namupha padooko pomwe pa Yordani; ndipo anagwa a Efuremu nthawi ija, zikwi makumi anai mphambu ziwiri.

7 Ndipo Yefita anaweruza Israele zaka zisanu ndi chimodzi; nafa Yefita Mgiliyadi, naikidwa m’mzinda wina wa Giliyadi.

Oweruza Ibzani, Eloni, Abidoni

8 Ndi pambuyo pake Ibizani wa ku Betelehemu anaweruza Israele.

9 Ndipo anali nao ana aamuna makumi atatu; ndi ana aakazi makumi atatu anawakwatitsa kwina, natengera ana ake aamuna ana aakazi makumi atatu ochokera kwina. Ndipo anaweruza Israele zaka zisanu ndi ziwiri.

10 Nafa Ibizani naikidwa ku Betelehemu.

11 Ndi pambuyo pake Eloni Mzebuloni anaweruza Israele; naweruza Israele zaka khumi.

12 Nafa Eloni Mzebuloni naikidwa mu Ayaloni m’dziko la Zebuloni.

13 Ndi pambuyo pake Abidoni mwana wa Hilele wa ku Piratoni anaweruza Israele.

14 Ndipo anali nao ana aamuna makumi anai ndi zidzukulu zazimuna makumi atatu, akuyenda okwera pa ana a abulu makumi asanu ndi awiri; naweruza Israele zaka zisanu ndi zitatu.

15 Nafa Abidoni mwana wa Hilele wa ku Piratoni, naikidwa mu Piratoni m’dziko la Efuremu ku mapiri a Amaleke.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/12-8ae42bd01ecd024ad60e37df43b83a4a.mp3?version_id=1068—