Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 33

Mose adalitsa mafuko 12 a Israele asanafe

1 Ndipo mdalitso, Mose munthu wa Mulungu anadalitsa nao ana a Israele asanafe, ndi uwu.

2 Ndipo anati,

Yehova anafuma ku Sinai,

nawatulukira ku Seiri;

anaoneka wowala paphiri la Parani,

anafumira kwa opatulika zikwizikwi;

ku dzanja lamanja lake kudawakhalira lamulo lamoto.

3 Inde akonda mitundu ya anthu;

opatulidwa ake onse ali m’dzanja mwanu;

ndipo akhala pansi ku mapazi anu;

yense adzalandirako mau anu.

4 Mose anatiuza chilamulo,

cholowa cha msonkhano wa Yakobo.

5 Ndipo Iye anali mfumu mu Yesuruni,

pakusonkhana mafumu a anthu,

pamodzi ndi mafuko a Israele.

6 Rubeni akhale ndi moyo, asafe,

koma amuna ake akhale owerengeka.

7 Za Yuda ndi izi; ndipo anati,

Imvani, Yehova, mau a Yuda,

ndipo mumfikitse kwa anthu ake;

manja ake amfikire;

ndipo mukhale inu thandizo lake pa iwo akumuukira.

8 Ndipo za Levi anati,

Tumimu ndi Urimu wanu zikhala ndi wokondedwa wanu,

amene mudamuyesa mu Masa,

amene mudalimbana naye ku madzi a Meriba;

9 amene anati za atate wake ndi amai wake,

sindinamuone; Sanazindikire abale ake,

sanadziwe ana ake omwe;

popeza anasamalira mau anu,

nasungachipanganochanu.

10 Adzaphunzitsa Yakobo maweruzo anu,

ndi Israele chilamulo chanu;

adzaika chofukiza pamaso panu,

ndi nsembe yopsereza yamphumphu paguwa la nsembe lanu.

11 Dalitsani, Yehova, mphamvu yake,

nimulandire ntchito ya manja ake;

akantheni m’chuuno iwo akumuukira,

ndi iwo akumuda, kuti asaukenso.

12 Za Benjamini anati,

Wokondedwa wa Yehova adzakhala ndi Iye mokhazikika;

am’phimba tsiku lonse,

inde akhalitsa pakati pa mapewa ake.

13 Ndipo za Yosefe anati,

Yehova adalitse dziko lake;

ndi zinthu zofunikatu za m’mwamba, ndi mame,

ndi madzi okhala pansipo;

14 ndi zipatso zofunikatu za dzuwa,

ndi zomera zofunikatu za mwezi,

15 ndi zinthu zoposa za mapiri akale,

ndi zinthu zofunikatu za zitunda zosatha,

16 ndi zinthu zofunikatu za dziko lapansi, ndi kudzala kwake,

ndi chivomerezo cha Iye anakhala m’chitsambayo.

Mdalitso ufike pamutu wa Yosefe,

ndi pakati pamutu wake wa iye wokhala padera ndi abale ake.

17 Woyamba kubadwa wa ng’ombe yake,

ulemerero ndi wake;

nyanga zake ndizo nyanga zanjati;

adzatunga nazo mitundu ya anthu pamodzi,

kufikira malekezero a dziko lapansi.

Iwo ndiwo zikwi khumi za Efuremu,

iwo ndiwo zikwi za Manase.

18 Ndi za Zebuloni anati,

Kondwera, Zebuloni, ndi kutuluka kwako;

ndi Isakara, m’mahema mwako.

19 Adzaitana mitundu ya anthu afike kuphiri;

apo adzaphera nsembe za chilungamo;

popeza adzayamwa zochuluka za m’nyanja,

ndi chuma chobisika mumchenga.

20 Ndi za Gadi anati,

Wodala iye amene akuza Gadi;

akhala ngati mkango waukazi,

namwetula dzanja, ndi pakati pamutu pomwe.

21 Ndipo anadzisankhira gawo loyamba,

popeza kumeneko kudasungika gawo la wolamulira;

ndipo anadza ndi mafumu a anthu,

anachita chilungamo cha Yehova,

ndi maweruzo ake ndi Israele.

22 Ndi za Dani anati,

Dani ndiye mwana wa mkango,

wakutumpha motuluka mu Basani.

23 Za Nafutali anati,

Nafutali, wokhuta nazo zomkondweretsa,

wodzala ndi mdalitso wa Yehova;

landira kumadzulo ndi kumwera.

24 Ndi za Asere anati,

Asere adalitsidwe mwa anawo;

akhale wovomerezeka mwa abale ake,

aviike phazi lake m’mafuta.

25 Nsapato zako zikhale za chitsulo ndi mkuwa;

ndipo monga masiku ako momwemo mphamvu yako.

26 Palibe wina ngati Mulungu, Yesuruni iwe,

wakuyenda wokwera pathambo, kukuthandiza,

ndi pa mitambo mu ukulu wake.

27 Mulungu wamuyaya ndiye mokhaliramo mwako;

ndi pansipo pali manja osatha.

Ndipo aingitsa mdani pamaso pako,

nati, Ononga.

28 Ndipo Israele akhala mokhazikika pa yekha;

kasupe wa Yakobo;

akhala m’dziko la tirigu ndi vinyo;

inde thambo lake likukha mame.

29 Wodala iwe, Israele;

akunga iwe ndani, mtundu wa anthu opulumutsidwa ndi Yehova,

ndiye chikopa cha thandizo lako,

Iye amene akhala lupanga la ukulu wako!

Ndi adani ako adzakugonjera;

ndipo udzaponda pa misanje yao.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/33-96067d5fd0fea14c74ad5ef2c29a65a8.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 34

Imfa ya Mose

1 Ndipo Mose anakwera kuchokera ku zidikha za Mowabu, kunka kuphiri la Nebo, pamwamba pa Pisiga, popenyana ndi Yeriko. Ndipo Yehova anamuonetsa dziko lonse la Giliyadi, kufikira ku Dani;

2 ndi Nafutali lonse, ndi dziko la Efuremu, ndi Manase, ndi dziko lonse la Yuda, kufikira nyanja ya m’tsogolo;

3 ndi kumwera, ndi chidikha cha chigwa cha Yeriko, mzinda wa migwalangwa, kufikira ku Zowari.

4 Ndipo Yehova anati kwa iye, Si ili dziko ndinalumbirira Abrahamu, Isaki ndi Yakobo, ndi kuti, Ndidzalipereka kwa mbeu zako. Ndinakuonetsa ili m’maso, koma sudzaolokako.

5 Ndipo Mose mtumiki wa Yehova anamwalirako m’dziko la Mowabu, monga mwa mau a Yehova.

6 Ndipo Iye anamuika m’chigwa m’dziko la Mowabu popenyana ndi Betepeori; koma palibe munthu wakudziwa kumanda kwake kufikira lero lino.

7 Ndipo zaka zake za Mose ndizo zana limodzi ndi makumi awiri, pakumwalira iye; diso lake silinachite mdima, ndi mphamvu yake siidaleke.

8 Ndipo ana a Israele analira Mose m’zidikha za Mowabu masiku makumi atatu; potero anatha masiku akulira maliro a Mose.

9 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anadzala ndi mzimu wanzeru; popeza Mose adamuikira manja ake; ndi ana a Israele anamvera iye, nachita monga Yehova adauza Mose.

10 Ndipo sanaukensomnenerimu Israele ngati Mose, amene Yehova anadziwana naye popenyana maso;

11 kunena za zizindikiro ndi zozizwa zonse zimene Yehova anamtumiza kuzichita m’dziko la Ejipito kwaFarao, ndi anyamata ake onse, ndi dziko lake lonse;

12 ndi kunena za dzanja la mphamvu lonse, ndi choopsa chachikulu chonse, chimene Mose anachita pamaso pa Israele wonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/34-e47aa763f7e2ea0c553b6abb35a66127.mp3?version_id=1068—

Categories
YOSWA

YOSWA Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli likukamba za m’mene Aisraele adalowera m’dziko la Kanani nkulilanda, Yoswa akuwatsogolera. Kenaka adagawana dzikolo.

Nkhani zodziwika bwino m’bukuli ndizo kuoloka Yordani, kugwa kwa Yeriko, kugonjetsedwa kwa Ai, ndi kukonzanso kwa chipangano pakati pa Mulungu ndi anthu ake.

Mau odziwika bwino ndi awa: “mudzisankhire lero amene mudzamtumikira…koma ine, ndi a m’nyumba yanga, tidzatumikira Yehova” (24.15).

Za mkatimu

Aisraele atenga dziko la Kanani

1.1—12.24

a. Aoloka mtsinje wa Yordani

1.1—5.15

b. Agonjetsa mzinda la Yeriko

6.1—7.26

c. Agonjetsa mzinda wa Ai ndi mizinda ina

8.1—12.24

Aisraele agawana dziko

13.1—22.34

a. Dziko la kum’mawa kwa Yordani

13.1-33

b. Dziko la kuzambwe kwa Yordani

14.1—19.51

c. Mizinda yopulumukirako

20.1-9

d. Mafuko awiri akum’mawa abwerera ku dziko lao

22.1-34

Mau a Yoswa otsanzikana nawo

23.1-16

Abwereza kuchita chipangano ku Sekemu

24.1-33

Categories
YOSWA

YOSWA 1

1 Ndipo atafa Mose mtumiki wa Yehova, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mnyamata wa Mose,

2 Mose mtumiki wanga wafa; tauka tsono, nuoloke Yordani uyu, iwe ndi anthu awa onse, kulowa m’dzikomo ndilikuwapatsa, ndiwo ana a Israele.

3 Pali ponse phazi lanu lidzapondapo ndinakupatsani, monga ndinanena ndi Mose.

4 Kuyambira chipululu, ndi Lebanoni uyu, kufikira mtsinje waukulu mtsinje wa Yufurate, dziko lonse la Ahiti, ndi kufikira Nyanja Yaikulu ku malowero a dzuwa, ndiwo malire anu.

5 Palibe munthu adzatha kuima pamaso pako masiku onse a moyo wako; monga ndinakhala ndi Mose momwemo ndidzakhala ndi iwe; sindidzakusowa, sindidzakusiya.

6 Khala wamphamvu, nulimbike mtima, pakuti udzagawira anthu awa dzikoli likhale cholowa chao, ndilo limene ndinalumbirira makolo ao kuwapatsa.

7 Komatu khala wamphamvu, nulimbike mtima kwambiri, kuti usamalire kuchita monga mwa chilamulo chonse anakulamuliracho Mose mtumiki wanga; usachipatukire ku dzanja lamanja kapena kulamanzere, kuti ukachite mwanzeru kulikonse umukako.

8 Buku ili la chilamulo lisachoke pakamwa pako; koma ulingiriremo usana ndi usiku, kuti usamalire kuchita monga mwa zonse zolembedwamo; popeza ukatero udzakometsa njira yako, nudzachita mwanzeru.

9 Kodi sindinakulamulire iwe? Khala wamphamvu, nulimbike mtima, usaope, kapena kutenga nkhawa, pakuti Yehova Mulungu wako ali ndi iwe kulikonse umukako.

10 Pamenepo Yoswa analamulira akapitao a anthu, ndi kuti,

11 Pitani pakati pa chigono, nimulamulire anthu, ndi kuti, Mudzikonzeretu kamba, pakuti asanapite masiku atatu mudzaoloka Yordani uyu, kulowa ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, likhale lanulanu.

12 Ndipo Yoswa anati kwa Arubeni, ndi Agadi, ndi hafu la fuko la Manase, ndi kuti,

13 Kumbukirani mau amene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulirani inu, kuti, Yehova Mulungu wanu akupatsani mpumulo, nadzakupatsani dziko lino.

14 Akazi anu, ana anu, ndi zoweta zanu zikhale m’dzikoli anakuninkhani Mose, tsidya lino la Yordani; koma inu muoloke okonzeka kunkhondo pamaso pa abale anu, ngwazi zonse, ndi kuwathandiza;

15 mpaka Yehova atapatsa abale anu mpumulo, monga umo anakuninkhirani inu, naonso alandira dzikolo awaninkha Yehova Mulungu wanu; pamenepo mubwerere ku dziko lanulanu, ndi kukhala nalo, limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya lino la Yordani la kum’mawa,

16 Ndipo anamyankha Yoswa, nati, Zonse mwatilamulira tidzachita, ndipo kulikonse mutitumako tidzamuka.

17 Monga momwe tinamvera mau onse a Mose momwemo tidzamvera inu; komatu akhale ndi inu Yehova Mulungu wanu monga anakhala ndi Mose.

18 Aliyense wakupikisana ndi inu, osamvera mau anu mulimonse mukamlamulira, aphedwe; komatu khalani wamphamvu, nimulimbike mtima.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/1-6b362df3be4ed66824cb37a3e37c2a5a.mp3?version_id=1068—

Categories
YOSWA

YOSWA 2

Yoswa atuma anthu awiri azonde Yeriko

1 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, ali ku Sitimu, anatuma amuna awiri mosadziwika kukazonda, ndi kuti, Mukani, mulipenye dzikolo, ndi ku Yeriko. Ndipo anamuka nalowa m’nyumba ya mkazi wadama, dzina lake Rahabi, nagona momwemo.

2 Ndipo wina anaiuza mfumu ya Yeriko, kuti, Taonani, usiku uno alowa muno amuna a ana a Israele, kulizonda dziko.

3 Ndipo mfumu ya Yeriko inatuma wina kwa Rahabi, ndi kuti, Tulutsa amunawo anafika kwanu, amene analowa m’nyumba mwako; popeza anadzera kulizonda dziko lonse.

4 Koma mkaziyo anatenga amuna awiriwo, nawabisa; natero, Inde, amunawo anandifikira; koma sindinadziwe uko afuma;

5 ndipo m’mene akadati atseke pachipata, kutada, anatuluka amunawo; uko anamuka amunawo osakudziwa ine; muwalondole msanga, pakuti mudzawapeza.

6 Koma adawakweretsa patsindwi, nawabisa ndi mitengo yanthamza yoyanika patsindwi.

7 Ndipo amunawo anawalondola panjira ya ku Yordani yonka kudooko; ndipo atatuluka akuwalondola, anatseka pachipata.

8 Koma asanagone iwo, anawakwerera patsindwi iye,

9 nati kwa amunawo, Ndidziwa kuti Yehova wakupatsani dzikoli, ndi kuti kuopsa kwanu kwatigwera, ndi kuti okhala m’dziko onse asungunuka pamaso panu.

10 Popeza tidamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a mu Nyanja Yofiira pamaso panu, muja mudatuluka mu Ejipito; ndi chija munachitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya la Yordani, ndiwo Sihoni ndi Ogi, amene mudawaononga konse.

11 Ndipo titamva ichi mitima yathu inasungunuka; analibenso mtima ndi mmodzi yense, chifukwa cha inu; pakuti Yehova Mulungu wanu, ndiye Mulungu wa m’mwamba umo, ndi padziko lapansi.

12 Ndipo tsopano, mundilumbiriretu kwa Yehova, popeza ndakuchitirani chifundo, kuti inunso mudzachitira chifundo a m’nyumba ya atate wanga ndi kundipatsa chizindikiro choona,

13 kuti mudzawasunga ndi moyo atate wanga ndi mai wanga, ndi alongo anga ndi abale anga, ndi zonse ali nazo, ndi kupulumutsa miyoyo yathu kuimfa.

14 Ndipo amunawo anati kwa iye, Moyo wathu ndiwo moyo wanu, mukapanda kuwulula chodzera ife; ndipo kudzakhala kuti, pakutipatsa ife dziko ili Yehova, tidzakuchitira chifundo ndi choonadi.

15 Pamenepo anawatsitsa pazenera ndi chingwe; popeza nyumba yake inali pa linga la mzinda, nakhala iye palingapo.

16 Ndipo anati kwa iwo, Mukani kuphiri, olondola angakupezeni; mubisale kumeneko masiku atatu, mpaka atabwerera olondolawo, pamenepo muyende ulendo wanu.

17 Ndipo amunawo anati kwa iye, Sitidzachimwira lumbiro lako ili watilumbiritsali.

18 Taona, tikadzalowa m’dzikomo ife, uzimanga chingwe ichi chofiira pazenera pamene watitsitsira; ndipo udzasonkhanitsa m’nyumbamo atate wako ndi mai wako ndi abale ako ndi a m’nyumba onse a atate wako.

19 Ndipo kudzakhala kuti aliyense akadzatuluka pa khomo la nyumba yako kubwalo, imfa imeneyi ndi yake, tilibe kupalamula ife; koma aliyense adzakhala ndi iwe m’nyumba, likamfikira dzanja, imfa imeneyi ndi yathu.

20 Koma ukawulula chodzera ifecho tidzamasukira lumbiro lako watilumbiritsali.

21 Nati iye, Momwemo, monga mwa mau anu. Ndipo anawauza amuke, iwo namuka; namanga iye chingwe chofiiracho pazenera.

22 Ndipo anayenda iwo, nafika kuphiri, nakhalako masiku atatu mpaka atabwerera olondolawo; popeza olondolawo anawafunafuna panjira ponse, osawapeza.

23 Pamenepo amuna awiriwo anabwerera, natsika m’phirimo naoloka, nafika kwa Yoswa mwana wa Nuni, namfotokozera zonse zidawagwera.

24 Ndipo anati kwa Yoswa, Zoonadi, Yehova wapereka dziko lonse m’manja mwathu; ndiponso nzika zonse zasungunuka pamaso pathu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/2-62ccc8efc30ba17f9b712f989a17f777.mp3?version_id=1068—

Categories
YOSWA

YOSWA 3

Aisraele aoloka Yordani

1 Ndipo Yoswa analawirira mamawa, kuchoka ku Sitimu, nafika ku Yordani, iye ndi ana onse a Israele; nagona komweko, asanaoloke.

2 Ndipo kunali atapita masiku atatu, akapitao anapita pakati pa chigono;

3 nalamulira anthu, ndi kuti, Mukadzaonalikasa la chipanganola Yehova Mulungu wanu, ndi ansembe Aleviwo atalisenza, pamenepo muchoke kwanu ndi kulitsata.

4 Koma pakhale dera pakati pa inu ndi ilo, monga mikono zikwi ziwiri poliyesa; musaliyandikire, kuti mudziwe njira imene muziyendamo; popeza simunapite njirayi kufikira lero.

5 Ndipo Yoswa ananena kwa anthu, Mudzipatule, pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati pa inu.

6 Ndipo Yoswa anati kwa ansembe, Senzani likasa la chipangano, nimuoloke pamaso pa anthu. Nasenza iwo likasa la chipangano, natsogolera anthu.

7 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, Lero lino ndidzayamba kukukuza pamaso pa Aisraele onse, kuti adziwe, kuti monga momwe ndinakhalira ndi Mose, momwemo ndidzakhala ndi iwe.

8 Ndipo uzilamulira ansembe akunyamula likasa la chipangano, ndi kuti, Pamene mufika kumphepete kwa madzi a Yordani muziima mu Yordani.

9 Ndipo Yoswa anati kwa ana a Israele, Idzani kuno, mumve mau a Yehova Mulungu wanu.

10 Nati Yoswa, Ndi ichi mudzadziwa kuti Mulungu wamoyo ali pakati pa inu, ndi kuti adzapirikitsa ndithu pamaso panu Akanani, ndi Ahiti, ndi Ahivi, ndi Aperizi, ndi Agirigasi, ndi Aamori, ndi Ayebusi.

11 Taonani, likasa la chipangano la Ambuye wa dziko lonse lapansi lioloka Yordani pamaso panu.

12 Ndipo tsono, mudzitengere amuna khumi ndi awiri mwa mafuko a Israele, fuko limodzi mwamuna mmodzi.

13 Ndipo kudzakhala, akaima mapazi a ansembe akusenza likasa la Yehova Ambuye wa dziko lonse, m’madzi a Yordani, adzadulidwa madziwo, ndiwo madzi ochokera kumagwero, nadzaima mulu umodzi.

14 Ndipo kunali pochoka anthu ku mahema ao kukaoloka Yordani, ansembe anasenza likasa la chipangano pamaso pa anthu.

15 Ndipo pamene iwo akusenza likasa anafika ku Yordani, nathibika m’mphepete mwa madzi mapazi a ansembe akusenza likasa, pakuti Yordani asefuka m’magombe ake onse, nyengo yonse ya masika,

16 pamenepo madzi ochokera kumagwero anaima, nauka ngati mulu, kutalitu ku Adama, ndiwo mzinda wa ku mbali ya Zaretani; koma madzi akutsikira kunka ku nyanja ya chidikha, ndiyo Nyanja ya Mchere, anadulidwa konse; ndipo anthu anaoloka pandunji pa Yeriko.

17 Ndipo ansembe akulisenza likasa la chipangano la Yehova, anaima pouma pakati pa Yordani, ndi Aisraele onse anaoloka pouma mpaka mtundu wonse unatha kuoloka Yordani.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/3-b0ba56b90b66acda86edc1e38b2604eb.mp3?version_id=1068—

Categories
YOSWA

YOSWA 4

Aimiritsa miyala 12 ikhale chikumbutso ku Giligala

1 Ndipo kunali, utatha kuoloka Yordani mtundu wonse, Yehova ananena ndi Yoswa, nati,

2 Mudzitengere mwa anthu, amuna khumi ndi awiri, fuko limodzi mwamuna mmodzi;

3 ndipo muwalamulire iwo ndi kuti, Mudzitengere pano pakati pa Yordani, poimapo mapazi a ansembe, miyala khumi ndi iwiri, ndi kuoloka nayo, ndi kuiika m’mogona m’mene mugonamo usiku uno.

4 Pamenepo Yoswa anaitana amuna khumi ndi awiriwo amene anawaikiratu mwa ana a Israele, fuko limodzi mwamuna mmodzi;

5 nanena nao Yoswa, Olokani, kutsogolera likasa la Yehova Mulungu wanu pakati pa Yordani, nimudzisenzere yense mwala paphewa pake, monga mwa kuwerenga kwa mafuko a ana a Israele;

6 kuti ichi chikhale chizindikiro pakati pa inu. Akakufunsani ana anu m’tsogolomo, ndi kuti, Miyala iyi nja chiyani ndi inu?

7 Munene nao, Chifukwa madzi a Yordani anadulidwa patsogolo palikasa la chipanganocha Yehova; muja lidaoloka Yordani, madzi a Yordani anadulidwa; ndipo miyala iyi idzakhala chikumbutso cha ana a Israele chikhalire.

8 Ndipo ana a Israele anachita monga Yoswa anawalamulira, nasenza miyala khumi ndi iwiri pakati pa Yordani, monga Yehova adalankhula ndi Yoswa, monga mwa kuwerenga kwa mafuko a ana a Israele; ndipo anaoloka nayo kunka kogona, naiika komweko.

9 Ndipo Yoswa anaimika miyala khumi ndi iwiri pakati pa Yordani, poimapo mapazi a ansembe akusenza likasa la chipangano; ikhala komweko kufikira lero lino.

10 Pakuti ansembe akusenza likasa anaima pakati pa Yordani, mpaka zitatha zonse Yehova adazilamulira Yoswa anene kwa anthu, monga mwa zonse Mose adalamulira Yoswa; ndipo anthu anafulumira kuoloka.

11 Ndipo kunali, atatha kuoloka anthu onse, likasa la Yehova linaoloka, ndi ansembe, pamaso pa anthu.

12 Ndipo ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi hafu la fuko la Manase anaoloka ndi zida zao pamaso pa ana a Israele, monga Mose adanena nao;

13 ngati zikwi makumi anai ankhondo okonzeka anaoloka pamaso pa Yehova kuthira nkhondo ku zidikha za Yeriko.

14 Tsiku lomwelo Yehova anakulitsa Yoswa pamaso pa Aisraele onse; ndipo anamuopa monga anaopa Mose, masiku onse a moyo wake.

15 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa,

16 Lamulira ansembe akusenza likasa la umboni, kuti akwere kutuluka mu Yordani.

17 Pamenepo Yoswa analamulira ansembe, ndi kuti, Kwerani kutuluka mu Yordani.

18 Ndipo kunali, atakwera ansembe akusenza likasa la chipangano la Yehova, kutuluka pakati pa Yordani, nakwera pamtunda mapazi a ansembe, madzi a mu Yordani anabwera m’njira mwake, nasefuka m’magombe ake onse monga kale.

19 Ndipo anthu anakwera kutuluka mu Yordani tsiku lakhumi la mwezi woyamba, namanga misasa ku Giligala, mbali ya ku m’mawa kwa Yeriko.

20 Ndipo Yoswa anaimika ku Giligala miyala ija khumi ndi iwiri adaitenga mu Yordani.

21 Ndipo anati kwa ana a Israele, Ana anu akadzafunsa atate ao masiku akudza, ndi kuti, Miyala iyi nja chiyani?

22 Pamenepo muzidziwitsa ana anu, ndi kuti, Israele anaoloka Yordani uyu pouma.

23 Pakuti Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yordani pamaso panu, mpaka mutaoloka; monga Yehova Mulungu wanu anachitira Nyanja Yofiira, imene anaiphwetsa pamaso pathu, mpaka titaoloka;

24 kuti mitundu yonse ya padziko lapansi idziwe dzanja la Yehova, kuti ndilo lamphamvu; kuti iope Yehova Mulungu wanu masiku onse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/4-f438774cf7afbf99465fb9017ed25607.mp3?version_id=1068—

Categories
YOSWA

YOSWA 5

Anthu adulidwa nachita Paska

1 Ndipo kunali, pamene mafumu onse a Aamori okhala tsidya la kumadzulo la Yordani, ndi mafumu onse a Akanani okhala ku nyanja anamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a Yordani pamaso pa ana a Israele mpaka titaoloka, mtima wao unasungunuka, analibenso moyo chifukwa cha ana a Israele.

2 Nthawi imeneyo Yehova anati kwa Yoswa, Udzisemere mipeni yamiyala nudulenso ana a Israele kachiwiri.

3 Ndipo Yoswa anadzisemera mipeni yamiyala nadula ana a Israele pa Gibea-Naraloti.

4 Koma chifukwa chakuti Yoswa anawadula ndi ichi: anthu onse otuluka mu Ejipito, anthu aamuna, ndiwo amuna onse ankhondo, adafa m’chipululu panjira, atatuluka mu Ejipito.

5 Pakuti anthu onse anatulukawo anadulidwa; koma anthu onse obadwa m’chipululu panjira potuluka mu Ejipito sanadulidwe.

6 Pakuti ana a Israele anayenda m’chipululu zaka makumi anai, mpaka mtundu wonse wa amuna ankhondo otuluka mu Ejipito udatha, chifukwa cha kusamvera mau a Yehova; ndiwo amene Yehova anawalumbirira kuti sadzawaonetsa dziko limene Yehova analumbirira makolo ao kudzatipatsa, ndilo dziko moyenda mkaka ndi uchi.

7 Koma ana ao aamuna amene anawautsa m’malo mwao, iwowa Yoswa anawadula; popeza anakhala osadulidwa, pakuti sanawadule panjira.

8 Ndipo kunali, atatha kudula mtundu wonse, anakhala m’malo mwao m’chigono mpaka adachira.

9 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, Lero lino ndakukunkhunizirani mtonzo wa Ejipito. Chifukwa chake dzina la malowo analitcha Giligala kufikira lero lino.

10 Ndipo ana a Israele anamanga misasa ku Giligala; nachitaPaskatsiku lakhumi ndi chinai la mwezi, madzulo, m’zidikha za Yeriko.

11 Ndipo m’mawa mwake atatha Paska, anadya tirigu wakhwimbi wa m’dziko, mikate yopanda chotupitsa ndi tirigu wokazinga tsiku lomwe lija.

12 Koma m’mawa mwakemanaanaleka, atadya iwo tirigu wakhwimbi wa m’dziko; ndipo ana a Israele analibenso mana; koma anadya zipatso za dziko la Kanani chaka chomwe chija.

Masomphenya a Yoswa

13 Ndipo kunali, pokhala Yoswa ku Yeriko, anakweza maso ake, napenya, ndipo taona, panaima munthu pandunji pake ndi lupanga lake losolola m’dzanja lake; namuka Yoswa kuli iye, nati iye, Uvomerezana ndi ife kapena ndi adani athu?

14 Nati, Iai, koma ndadza ine, kazembe wa ankhondo a Yehova. Pamenepo Yoswa anagwa nkhope yake pansi, napembedza, nati kwa iye, Anenanji Ambuyanga kwa mtumiki wake?

15 Ndipo kazembe wa ankhondo a Yehova anati kwa Yoswa, Vula nsapato yako pa phazi lako; pakuti malo upondapo mpopatulika. Nachita Yoswa chomwecho.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/5-b2f11255df9488808d2cc8a8666a0aea.mp3?version_id=1068—

Categories
YOSWA

YOSWA 6

Kupasulidwa kwa Yeriko

1 Koma ku Yeriko anatseka pazipata, natsekedwa chifukwa cha ana a Israele, panalibe wotuluka, panalibenso wolowa.

2 Ndipo Yehova ananena kwa Yoswa, Taona, ndapereka m’dzanja lako Yeriko ndi mfumu yake, ndi ngwazi zake.

3 Ndipo muzizungulira mzinda inu nonse ankhondo, kuuzungulira mzinda kamodzi. Muzitero masiku asanu ndi limodzi.

4 Ndipo ansembe asanu ndi awiri azinyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo, natsogolere nazo likasa; koma tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzizungulira mzindawo kasanu ndi kawiri, ndi ansembe aziliza mphalasazo.

5 Ndipo kudzakhala kuti akaliza chilizire ndi nyanga ya nkhosa yamphongo, nimumva kulira kwa mphalasa, anthu onse afuule mfuu yaikulu; ndipo linga la mzindawo lidzagwa pomwepo, ndi anthu adzakwera ndi kulowamo yense kumaso kwake.

6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anaitana ansembe, nanena nao, Senzanilikasa la chipangano, ndi ansembe asanu ndi awiri anyamule mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo, kutsogolera nazo likasa la Yehova.

7 Nati kwa anthu, Pitani, muzizungulira mzinda, ndi ankhondo ndi zida zao atsogolere likasa la Yehova.

8 Ndipo atanena kwa anthu Yoswa, ansembe asanu ndi awiri akunyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo pamaso pa Yehova, anapita naliza mphalasazo; ndipo likasa la chipangano cha Yehova linawatsata.

9 Ndipo okonzeka kunkhondo anatsogolera ansembe akuliza mphalasa, koma akudza m’mbuyo anatsata likasa, ansembe ali chiombere poyenda iwo.

10 Ndipo Yoswa analamulira anthu, ndi kuti, Musamafuula, kapena kumveketsa mau anu, asatuluke konse mau m’kamwa mwanu, mpaka tsiku lakunena nanu ine, Fuulani; pamenepo muzifuula.

11 Ndipo anazungulitsa likasa la Yehova mzinda, kuzungulira kamodzi; pamenepo analowa kuchigono, nagona m’mwemo.

12 Ndipo Yoswa analawira mamawa, ndi ansembe anasenza likasa la Yehova.

13 Ndipo ansembe asanu ndi awiri, akunyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo ndi kutsogolera nazo likasa la Yehova, anayenda chiyendere naliza mphalasazo; ndi okonzeka kunkhondowo anawatsogolera, ndi akudza m’mbuyo anatsata likasa la Yehova, ansembe ali chiombere poyenda iwo.

14 Ndipo tsiku lachiwiri anazungulira mzinda kamodzi, nabwera kuchigono; anatero masiku asanu ndi limodzi.

15 Ndipo kunali, tsiku lachisanu ndi chiwiri analawira mamawa, mbandakucha, nazungulira mzinda mommuja kasanu ndi kawiri; koma tsiku lijalo anazungulira mzinda kasanu ndi kawiri.

16 Ndipo kunali, pa nthawi yachisanu ndi chiwiri, pamene ansembe analiza mphalasa, Yoswa anati kwa anthu, Fuulani; pakuti Yehova wakupatsani mzindawo.

17 Koma mzindawo udzaperekedwa kwa Yehova ndi kuonongeka konse, uwu ndi zonse zili m’mwemo; Rahabi yekha wadamayo adzakhala ndi moyo, iye ndi onse ali naye m’nyumba, chifukwa anabisa mithenga tinawatumawo.

18 Ndipo inu, musakhudze choperekedwacho, mungadziononge konse, potapa choperekedwacho; ndi kuononga konse chigono cha Israele ndi kuchisautsa.

19 Komasilivayense, ndi golide yense, ndi zotengera za mkuwa ndi chitsulo zikhala chopatulikira Yehova; zilowe m’mosungira chuma cha Yehova.

20 Ndipo anthu anafuula, naliza mphalasa ansembe; ndipo kunali, pamene anthu anamva kulira kwa mphalasa, anafuula anthu ndi mfuu yaikulu, niligwa linga pomwepo; nakwera anthu kulowa m’mzinda, yense kumaso kwake; nalanda mzindawo.

Apulumutsidwa Rahabi

21 Ndipo anapereka kuziononga ndi lupanga lakuthwa zonse za m’mzinda, amuna ndi akazi omwe, ana ndi nkhalamba zomwe, kudza ng’ombe, ndi nkhosa, ndi abulu, ndi lupanga lakuthwa.

22 Ndipo Yoswa ananena kwa amuna awiri anazonda dzikowo, Lowani m’nyumba ya mkazi wadamayo, ndi kutulutsamo mkaziyo ndi zonse ali nazo, monga munamlumbirira iye.

23 Pamenepo anyamata ozondawo analowa, natulutsa Rahabi, ndi atate wake ndi mai wake ndi abale ake, ndi onse anali nao; anatulutsanso achibale ake onse; nawaika kunja kwa chigono cha Israele.

24 Ndipo anatentha mzinda ndi moto, ndi zonse zinali m’mwemo; koma siliva ndi golide ndi zotengera zamkuwa ndi zachitsulo anaziika m’mosungira chuma cha nyumba ya Yehova.

25 Koma Rahabi, mkazi wadamayo ndi banja la atate wake, ndi onse anali nao, Yoswa anawasunga ndi moyo; ndipo anakhala pakati pa Israele mpaka lero lino; chifukwa anabisa mithenga imene Yoswa anaituma kuzonda Yeriko.

26 Ndipo Yoswa anawalumbirira nyengo ija, ndi kuti, Wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzauka ndi kumanga mzinda uwu wa Yeriko; adzamanga maziko ake ndi kutayapo mwana wake woyamba, nadzaimika zitseko zake ndi kutayapo mwana wake wotsirizira.

27 Potero Yehova anakhala ndi Yoswa; ndi mbiri yake inabuka m’dziko lonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/6-377a297cb3168c6f4e263aaf50c6f9da.mp3?version_id=1068—

Categories
YOSWA

YOSWA 7

Kuchimwa kwa Akani

1 Koma ana a Israele analakwa ndi choperekedwacho; popeza Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda, anatapa choperekedwacho; ndi mkwiyo wa Yehova unayakira ana a Israele.

2 Ndipo Yoswa anatuma amuna kuchokera ku Yeriko apite ku Ai, ndiwo pafupi pa Betaveni, kum’mawa kwa Betele; nanena nao, Kwerani ndi kukazonda dziko. Nakwera amunawo, nazonda Ai.

3 Ndipo anabwera kwa Yoswa, nati kwa iye, Asakwere anthu onse; koma akwere amuna ngati zikwi ziwiri kapena zitatu kukantha Ai; musalemetsa anthu onse kunkako, pakuti a komweko ndi owerengeka.

4 Potero mwa anthu anakwerako amuna monga zikwi zitatu; koma anathawa pamaso pa amuna a ku Ai.

5 Ndipo amuna a ku Ai anawakantha amuna, ngati makumi atatu mphambu asanu ndi mmodzi; nawapirikitsa kuyambira pachipata mpaka ku Sebarimu, nawakantha potsika; ndi mitima ya anthu inasungunuka inga madzi.

6 Ndipo Yoswa anang’amba zovala zake, nagwa nkhope yake pansi, ku likasa la Yehova, mpaka madzulo, iye ndi akuluakulu a Israele, nathira fumbi pamitu pao.

7 Ndipo Yoswa anati, Ha! Ambuye, Yehova, mwaolotseranji anthu awa pa Yordani, kutipereka ife m’dzanja la Aamori, kutiononga ife? Mwenzi titalola ndi kukhala tsidya lija la Yordani!

8 Ndidzanenanji, Ambuye, Israele atabwerera m’mbuyo pamaso pa adani ao?

9 Akadzamva ichi Akanani ndi okhala m’dziko onse, adzatizinga ndi kuduliratu dzina lathu padziko lapansi; ndipo mudzachitiranji dzina lanu lalikulu?

10 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, Tauka, wagweranji pankhope pako chotere?

11 Israele wachimwa, nalakwiransochipanganochanga, ndinawalamuliracho; natengakonso choperekedwacho; anabanso, nanyenganso, nachiika pakati pa akatundu ao.

12 Mwa ichi ana a Israele sangathe kuima pamaso pa adani ao, awafulatira adani ao, pakuti aperekedwa aonongeke. Sindidzakhalanso nanu mukapanda kuononga choperekedwacho, kuchichotsa pakati pa inu.

13 Tauka, patula anthu, nuti, Mudzipatulire mawa; pakuti atero Yehova Mulungu wa Israele, Pali choperekedwa chionongeke pakati pako, Israele iwe; sungathe kuima pamaso pa adani ako, mpaka mutachotsa choperekedwacho pakati panu.

14 Koma m’mawa adzakuyandikitsani, fuko ndi fuko; ndipo kudzali kuti fukoli Yehova aliwulula lidzayandikira mwa zibale zake; ndi chibale Yehova achiwulula chidzayandikira monga mwa a nyumba ake; ndi a m’nyumbawo Yehova awawulula adzayandikira mmodzimmodzi.

15 Ndipo kudzali kuti iye wogwidwa ali nacho choperekedwacho adzatenthedwa ndi moto, iye ndi zonse ali nazo chifukwa analakwira chipangano cha Yehova, ndi chifukwa anachita chopusa mu Israele.

16 Ndipo Yoswa analawira mamawa, nayandikizitsa Israele, fuko ndi fuko; ndi fuko la Yuda linagwidwa;

17 nayandikizitsa zibale za Yuda, nagwira chibale cha Azera; nayandikizitsa chibale cha Azera, mmodzimmodzi, nagwidwa Zabidi;

18 nayandikizitsa a m’nyumba yake mmodzimmodzi; ndipo Akani, mwana wa Karimi, mwanu wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anagwidwa.

19 Ndipo Yoswa anati kwa Akani, Mwana wanga, uchitiretu ulemu Yehova Mulungu wa Israele, numlemekeze Iye; nundiuze tsopano, wachitanji? Usandibisire.

20 Ndipo Akani anayankha Yoswa nati, Zoonadi, ndachimwira Yehova Mulungu wa Israele, ndachita zakutizakuti;

21 pamene ndinaona pazofunkha malaya abwino a ku Babiloni, ndi masekeli mazana awiri asiliva, ndi chikute chagolide, kulemera kwake masekeli makumi asanu, ndinazikhumbira ndi kuzitenga; ndipo taonani, ndazibisa m’nthaka pakati pa hema wanga, ndi siliva pansi pakepo.

22 Pamenepo Yoswa anatuma mithenga, iwo nathamangira kuhema; ndipo taonani, zidabisika m’hema mwake ndi siliva pansi pake.

23 Ndipo anazichotsa pakati pa hema, nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa ana onse a Israele, nazitula pamaso pa Yehova.

24 Ndipo Yoswa, ndi Aisraele onse naye, anatenga Akani mwana wa Zera, ndi siliva, ndi malayawo, ndi chikute chagolide, ndi ana ake aamuna ndi aakazi, ndi ng’ombe zake, ndi abulu ake, ndi nkhosa zake, ndi hema wake ndi zake zonse; nakwera nazo ku chigwa cha Akori.

25 Ndipo Yoswa anati, Watisautsiranji? Yehova adzakusautsa lero lino. Ndipo Aisraele onse anamponya miyala, nawatentha ndi moto, nawaponya miyala.

26 Ndipo anamuunjikira mulu waukulu wamiyala, wokhalako kufikira lero lino; ndipo Yehova anatembenuka kusiya mkwiyo wake waukulu. Chifukwa chake anatcha dzina lake la malowo, Chigwa cha Akori, mpaka lero lino.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/7-ef0e3588cccc4dbc6d15db8a8ddfb710.mp3?version_id=1068—