Categories
LUKA

LUKA 16

Fanizo la kapitao wonyenga

1 Ndipo Iye ananenanso kwaophunziraake, Panali munthu mwini chuma, anali ndi kapitao wake; ndipo ameneyu ananenezedwa kwa iye kuti alikumwaza chuma chake.

2 Ndipo anamuitana, nati kwa iye, Ichi ndi chiyani ndikumva za iwe? Undiwerengere za ukapitao wako; pakuti sungathe kukhalabe kapitao.

3 Ndipo kapitao uyu anati mumtima mwake, Ndidzachita chiyani, chifukwa mbuye wanga andichotsera ukapitao? Kulima ndilibe mphamvu, kupemphapempha kundichititsa manyazi.

4 Ndidziwa chimene ndidzachita, kotero kuti pamene ananditulutsa muukapitao, anthu akandilandire kunyumba kwao.

5 Ndipo anadziitanira mmodzi ndi mmodzi amangawa onse a mbuye wake, nanena kwa woyamba, Unakongola chiyani kwa mbuye wanga?

6 Ndipo anati, Mitsuko ya mafuta zana. Ndipo iye ananena naye, Tenga kalata yako, nukhale pansi msanga, nulembere, Makumi asanu.

7 Pomwepo anati kwa wina, Ndipo iwe uli nao mangawa otani? Ndipo uyu anati, Madengu a tirigu zana. Iye ananena naye, Tenga kalata yako nulembere makumi asanu ndi atatu.

8 Ndipo mbuye wake anatama kapitao wonyengayo, kuti anachita mwanzeru; chifukwa ana a nthawi ya pansi pano ali anzeru m’mbadwo wao koposa ana a kuunika.

9 Ndipo Ine ndinena kwa inu, Mudziyesere nokha abwenzi ndi chuma chosalungama; kuti pamene chikakusowani, iwo akalandire inu m’mahema osatha.

10 Iye amene akhulupirika m’chaching’onong’ono alinso wokhulupirika m’chachikulu; ndipo iye amene ali wosalungama m’chachikulu.

11 Chifukwa chake ngati simunakhale okhulupirika m’chuma cha chosalungama, adzakhulupirira inu ndani ndi chuma choona?

12 Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi zake za wina, adzakupatsani inu ndani za inu eni?

13 Palibe mnyamata wa m’nyumba akhoza kukhala kapolo wa ambuye awiri; pakuti kapena adzamuda wina, nadzakonda winayo; kapena adzatsata wina, nadzapeputsa winayo. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa Chuma.

Za mphamvu ya chilamulo

14 KomaAfarisi, ndiwo okonda ndalama, anamva izi zonse; ndipo anamseka.

15 Ndipo anati kwa iwo, Inu ndinu odziyesera nokha olungama pamaso pa anthu; koma Mulungu azindikira mitima yanu; chifukwa ichi chimene chikuzika mwa anthu chili chonyansa pamaso pa Mulungu.

16 Chilamulo ndi aneneri analipo kufikira pa Yohane; kuyambira pamenepo ulalikidwa Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu, ndipo munthu aliyense akangamira kulowamo.

17 Kuti thambo ndi dziko lapansi zichoke nkwapafupi, koma kuti kalembo kakang’ono kachilamulo kagwe nkwapatali.

18 Yense wakusudzula mkazi wake, nakwatira wina, achita chigololo; ndipo iye amene akwatira wosudzulidwayo, achita chigololo.

Fanizo la mwini chuma ndi Lazaro waumphawi

19 Ndipo panali munthu mwini chuma amavala chibakuwa ndi nsalu yabafuta, nasekera, nadyerera masiku onse;

20 ndipo wopemphapempha wina, dzina lake Lazaro, adaikidwa pakhomo pake wodzala ndi zilonda,

21 ndipo anafuna kukhuta ndi zakugwa pa gome la mwini chumayo; komatu agalunso anadza nanyambita zilonda zake.

22 Ndipo kunali kuti wopemphayo adafa, ndi kuti anatengedwa iye ndiangelokunka kuchifuwa cha Abrahamu; ndipo mwini chumayo adafanso, naikidwa m’manda.

23 Ndipo m’dziko la akufa anakweza maso ake, pokhala nao mazunzo, naona Abrahamu patali, ndi Lazaro m’chifuwa mwake.

24 Ndipo anakweza mau nati, Atate Abrahamu, mundichitire chifundo, mutume Lazaro, kuti aviike nsonga ya chala chake m’madzi, naziziritse lilime langa; pakuti ndizunzidwadi m’lawi ili la moto.

25 Koma Abrahamu anati, Mwana, kumbukira kuti unalandira zokoma zako pakukhala m’moyo iwe, momwemonso Lazaro zoipa; ndipo tsopano iye asangalatsidwa pano, koma iwe uzunzidwadi.

26 Ndipo pamwamba pa izi, pakati pa ife ndi inu pakhazikika phompho lalikulu, kotero kuti iwo akufuna kuoloka kuchokera kuno kunka kwa inu sangathe, kapena kuchokera kwanuko kuyambuka kudza kwa ife, sangathenso.

27 Koma anati, Pamenepo ndikupemphani, Atate, kuti mumtume kunyumba ya atate wanga;

28 pakuti ndili nao abale asanu; awachitire umboni iwo kuti iwonso angadze kumalo ano a mazunzo.

29 Koma Abrahamu anati, Ali ndi Mose ndi aneneri; amvere iwo.

30 Koma anati, Iai, Atate Abrahamu, komatu ngati wina akapita kwa iwo wochokera kwa kufa adzasandulika mtima.

31 Koma anati kwa iye, Ngati samvera Mose ndi aneneri, sadzakopeka mtima ngakhale wina akauka kwa akufa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/16-a025e8f9dafb364a80bbb8e7b5343d27.mp3?version_id=1068—

Categories
LUKA

LUKA 17

Za zolakwitsa, ndi makhululukidwe, ndi mphamvu ya chikhulupiriro ndi kutumikira kwathu

1 Ndipo anati kwaophunziraake, Sikutheka kuti zolakwitsa zisadze; koma tsoka iye amene adza nazo.

2 Kukolowekedwa mwala wamphero m’khosi mwake ndi kuponyedwa iye m’nyanja nkwapafupi, koma kulakwitsa mmodzi wa ang’ono awa nkwapatali.

3 Kadzichenjerani nokha; akachimwa mbale wako umdzudzule, akalapa, umkhululukire.

4 Ndipo akakuchimwira kasanu ndi kawiri pa tsiku lake, nakakutembenukira kasanu ndi kawiri ndi kunena, Ndalapa ine; uzimkhululukira.

5 Ndipoatumwianati kwa Ambuye, Mutionjezere chikhulupiriro.

6 Koma Ambuye anati, Mukakhala nacho chikhulupiriro ngati kambeu kampiru, mukanena kwa mtengo uwu wamkuyu, Uzulidwe, nuokedwe m’nyanja; ndipo ukadamvera inu.

7 Koma ndani mwa inu ali naye kapolo wolima, kapena woweta nkhosa, amene pobwera iye kuchokera kumunda adzanena kwa iye, Lowa tsopano, khala pansi kudya;

8 wosanena naye makamaka, Undikonzere chakudya ine, nudzimangire, nunditumikire kufikira ndadya ndi kumwa; ndipo nditatha ine udzadya nudzamwa iwe?

9 Kodi ayamika kapoloyo chifukwa anachita zolamulidwa?

10 Chotero inunso m’mene mutachita zonse anakulamulirani, nenani, Ife ndife akapolo opanda pake, tangochita zimene tayenera kuzichita.

Yesu achiritsa akhate khumi

11 Ndipo kunali, pakumuka kuYerusalemuIye analikupita pakati pa Samariya ndi Galileya.

12 Ndipo m’mene analowa Iye m’mudzi wina, anakomana naye amuna khumi akhate, amene anaima kutali;

13 ndipo iwo anakweza mau, nanena, Yesu, Mbuye, mutichitire chifundo.

14 Ndipo pakuwaona anati kwa iwo, Pitani, kadzionetseni nokha kwa ansembe. Ndipo kunali, m’kumuka kwao, anakonzedwa.

15 Ndipo mmodzi wa iwo, pakuona kuti anachiritsidwa, anabwerera m’mbuyo, nalemekeza Mulungu ndi mau aakulu;

16 ndipo anagwa nkhope yake pansi kumapazi ake, namyamika Iye; ndipo analiMsamariyaameneyo.

17 Ndipo Yesu anayankha nati, Kodi sanakonzedwe khumi? Koma ali kuti asanu ndi anai aja?

18 Akubwera kulemekeza Mulungu sanapezeke mmodzi kodi, koma mlendo uyu?

19 Ndipo anati kwa iye, Nyamuka, nupite; chikhulupiriro chako chakupulumutsa iwe.

Za kufikanso kwa Ambuye

20 Ndipo pameneAfarisianamfunsa Iye, kuti, Ufumu wa Mulungu ukudza liti, anawayankha, nati, Ufumu wa Mulungu sukudza ndi maonekedwe;

21 ndipo sadzanena, Taonani uwu, kapena uwo! Pakuti, taonani, Ufumu wa Mulungu uli m’kati mwa inu.

22 Ndipo anati kwa ophunzira ake, Adzadza masiku, amene mudzakhumba kuona limodzi la masiku aMwana wa Munthu, koma simudzaliona.

23 Ndipo adzanena ndi inu, Taonani ilo! Taonani ili? Musachoka kapena kuwatsata;

24 pakuti monga mphezi ing’anipa kuchokera kwina pansi pa thambo, niunikira kufikira kwina pansi pa thambo, kotero adzakhala Mwana wa Munthu m’tsiku lake.

25 Koma ayenera ayambe wamva zowawa zambiri nakanidwe ndi mbadwo uno.

26 Ndipo monga kunakhala masiku a Nowa, momwemo kudzakhalanso masiku a Mwana wa Munthu.

27 Anadya, anamwa, anakwatira, anakwatiwa, kufikira tsiku lija Nowa analowa m’chingalawa, ndipo chinadza chigumula, nkuwaononga onsewo.

28 Monga momwenso kunakhala masiku a Loti; anadya, anamwa, anagula, anagulitsa, anabzala, anamanga nyumba;

29 koma tsiku limene Loti anatuluka mu Sodomu udavumba moto ndisulufurezochokera kumwamba, ndipo zinawaononga onsewo;

30 momwemo kudzakhala tsiku lakuvumbuluka Mwana wa Munthu.

31 Tsikulo iye amene adzakhala pamwamba pa tsindwi, ndi akatundu ake m’nyumba, asatsike kuwatenga; ndipo iye amene ali m’munda modzimodzi asabwere ku zake za m’mbuyo.

32 Kumbukirani mkazi wa Loti.

33 Iye aliyense akafuna kusunga moyo wake adzautaya, koma iye aliyense akautaya, adzausunga.

34 Ndinena ndi inu, usiku womwewo adzakhala awiri pa kama mmodzi; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.

35 Padzakhala akazi awiri akupera pamodzi, mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.

37 Ndipo anayankha nanena kwa Iye, Kuti, Ambuye? Ndipo anati kwa iwo, Pamene pali mtembo, pomweponso miimba idzasonkhanidwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/17-8aaea162cdb9799223cee29e0895bfe8.mp3?version_id=1068—

Categories
LUKA

LUKA 18

Fanizo la woweruza wosalungama

1 Ndipo anawanenerafanizolakuti ayenera iwo kupemphera nthawi zonse, osafooka mtima;

2 nanena, M’mzinda mwakuti munali woweruza wosaopa Mulungu, ndi wosasamala munthu.

3 Ndipo m’mzinda momwemo munali mkazi wamasiye; ndipo anadza kwa iye nanena, Mundiweruzire mlandu pa wotsutsana nane.

4 Ndipo sanafune nthawi; koma bwinobwino anati mwa yekha, Ndingakhale sindiopa Mulungu kapena kusamala munthu;

5 koma chifukwa cha kundivuta ine mkazi wamasiye amene ndidzamweruzira mlandu, kuti angandilemetse ndi kudzaidza kwake.

6 Ndipo Ambuye anati, Tamverani chonena woweruza wosalungama.

7 Ndipo kodi Mulungu sadzachitira chilungamo osankhidwa ake akumuitana usana ndi usiku, popeza aleza nao mtima?

8 Ndinena ndi inu, adzawachitira chilungamo posachedwa. KomaMwana wa Munthupakudza Iye, adzapeza chikhulupiriro padziko lapansi kodi?

Fanizo la Mfarisi ndi wamsonkho

9 Ndipo anatinso kwa ena amene anadzikhulupirira mwa iwo okha kuti ali olungama, napeputsa onse ena, fanizo ili,

10 Anthu awiri anakwera kunka ku Kachisi kukapemphera; winayoMfarisindi mnzakewamsonkho.

11 Mfarisiyo anaimirira napemphera izi mwa yekha,Mulungu, ndikuyamikani kuti sindili monga anthu onse ena, opambapamba, osalungama, achigololo, kapenanso monga wamsonkho uyu;

12 ndisala chakudya kawiri sabata limodzi; ndipereka limodzi la magawo khumi la zonse ndili nazo.

13 Koma wamsonkhoyo alikuima patali sanafune kungakhale kukweza maso kumwamba, komatu anadziguguda pachifuwa pake nanena, Mulungu, mundichitire chifundo, ine wochimwa.

14 Ndinena ndi inu, anatsikira kunyumba kwake woyesedwa wolungama uyutu, wosati uja ai; pakuti yense wakudzikuza yekha adzachepetsedwa; koma wodzichepetsa yekha adzakulitsidwa.

Yesu adalitsa ana

15 Ndipo anadza nao kwa Iye ana amakanda kuti awakhudze; koma pameneophunziraanaona anawadzudzula.

16 Koma Yesu anawaitana, nanena, Lolani ana adze kwa Ine, ndipo musawaletse; pakuti Ufumu wa Mulungu uli wa otere.

17 Indetu ndinena kwa inu, Aliyense wosalandira Ufumu wa Mulungu ngati mwana, sadzalowamo ndithu.

Mkulu mwini chuma

18 Ndipo mkulu wina anamfunsa Iye, nanena, Mphunzitsi wabwino, ndizichita chiyani, kuti ndilowe moyo wosatha?

19 Koma Yesu anati kwa iye, Unditcha Ine wabwino bwanji? Palibe wabwino, koma mmodzi, ndiye Mulungu.

20 Udziwa malamulo. Usachite chigololo, Usaphe, Usabe, Usachite umboni wonama, Lemekeza atate wako ndi amai ako.

21 Koma anati, Izi zonse ndazisunga kuyambira ubwana wanga.

22 Koma m’mene Yesu anamva, anati kwa iye, Usowa chinthu chimodzi: gulitsa zilizonse uli nazo, nugawire osauka; ndipo udzakhala nacho chuma chenicheni mu Mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

23 Koma pakumva izi anagwidwa nacho chisoni chambiri; pakuti anali mwini chuma chambiri.

24 Ndipo Yesu pomuona iye anati, Ha! Nkuvutika nanga kwa anthu eni chuma kulowa Ufumu wa Mulungu!

25 Pakuti nkwapafupi kwangamiraipyole diso la singano koma kwa munthu mwini chuma, kulowa Ufumu wa Mulungu nkwapatali.

26 Koma akumvawo anati, Tsono ndani angathe kupulumutsidwa?

27 Koma Iye anati, Zinthu zosatheka ndi anthu zitheka ndi Mulungu.

28 Ndipo Petro anati, Taonani ife tasiya zathu za ife eni, ndipo takutsatani Inu.

29 Koma anati kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, Palibe munthu wasiya nyumba, kapena mkazi, kapena abale, kapena akum’bala, kapena ana, chifukwa cha Ufumu wa Mulungu,

30 koma adzalandira zobwezedwa koposatu m’nthawi ino; ndipo m’nthawi ilinkudza moyo wosatha.

Yesu aneneratu za mazunzo ake

31 Ndipo anadzitengera khumi ndi awiriwo, nati kwa iwo, Taonani, tikwera kunka kuYerusalemu, ndipo zidzakwaniritsidwa kwa Mwana wa Munthu zonse zolembedwa ndi aneneri.

32 Pakuti adzampereka kwaamitundu, nadzamseka, nadzamchitira chipongwe, nadzamthira malovu;

33 ndipo atamkwapula adzamupha Iye; ndipo tsiku lachitatu adzauka.

34 Ndipo sanadziwitse kanthu ka izi; ndi mau awa adawabisikira, ndipo sanazindikire zonenedwazo.

Msaona wa ku Yeriko

35 Ndipo kunali, pamene anayandikira ku Yeriko, msaona wina anakhala m’mbali mwa njira, napemphapempha;

36 ndipo pakumva khamu la anthu alinkupita, anafunsa, Ichi nchiyani?

37 Ndipo anamuuza iye, kuti, Yesu Mnazarayo alinkupita.

38 Ndipo anafuula, nanena, Yesu, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo.

39 Ndipo iwo akutsogolera anamdzudzula iye, kuti akhale chete; koma iye anafuulitsa chifuulire, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo.

40 Ndipo Yesu anaima, nalamulira kuti abwere naye kwa Iye; ndipo m’mene adafika pafupi, anamfunsa iye,

41 Ufuna ndikuchitire chiyani? Ndipo anati, Ambuye, kuti ndipenyenso.

42 Ndipo Yesu anati kwa iye, Penyanso: chikhulupiriro chako chakupulumutsa iwe.

43 Ndipo pomwepo anapenyanso, namtsata Iye, ndi kulemekeza Mulungu: ndipo anthu onse pakuona, anachitira Mulungu mayamiko.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/18-177d6c72454fe99c76e4209c6b65fd18.mp3?version_id=1068—

Categories
LUKA

LUKA 19

Zakeyo asandulika mtima

1 Ndipo analowa, napyola pa Yeriko.

2 Ndipo taonani, mwamuna wotchedwa dzina lake Zakeyo; ndipo iye anali mkulu waamisonkho, nali wachuma.

3 Ndipo anafuna kuona Yesu ndiye uti, ndipo sanathe, chifukwa cha khamulo, pakuti anali wamfupi msinkhu.

4 Ndipo anathamanga, natsogola, nakwera mumkuyu kukamuona Iye; pakuti anati apite njira yomweyi.

5 Ndipo m’mene anadza pamalopo Yesu anakweza maso nati kwa iye, Zakeyo, fulumira, nutsike; pakuti lero ndiyenera kukhala m’nyumba mwako.

6 Ndipo anafulumira, natsika, namlandira Iye wokondwera.

7 Ndipo m’mene anachiona anadandaula onse, nanena, Analowa amchereze munthu ali wochimwa.

8 Ndipo Zakeyo anaimirira nati kwa Ambuye, Taonani, Ambuye, gawo limodzi la zanga zonse zogawika pakati ndipatsa osauka; ndipo ngati ndalanda kanthu kwa munthu monyenga, ndimbwezera kanai.

9 Ndipo Yesu anati kwa iye, Lero chipulumutso chagwera nyumba iyi, popeza iyenso ndiye mwana wa Abrahamu.

10 PakutiMwana wa Munthuanadza kufunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.

Fanizo la ndalama khumi za mina

11 Ndipo pakumva izi iwo, Iye anaonjeza nanenafanizo, chifukwa anali Iye pafupi paYerusalemu, ndipo iwo anayesa kuti Ufumu wa Mulungu ukuti uonekere pomwepo.

12 Pamenepo anati, Munthu wa fuko lomveka ananka kudziko lakutali, kudzilandirira yekha ufumu, ndi kubwerako.

13 Ndipo anaitana akapolo ake khumi, nawapatsa iwo ndalama khumi za mina, nati kwaiwo, Chita nazoni malonda kufikira ndibweranso.

14 Koma mfulu za pamudzi pake zinamuda, nkutuma akazembe amtsate m’mbuyo ndi kunena, Ife sitifuna munthuyo akhale mfumu yathu.

15 Ndipo kunali, pakubwera iye, atalandira ufumuwo, anati aitanidwe kwa iye akapolo aja, amene adawapatsa ndalamazo, kuti adziwe umo anapindulira pochita malonda.

16 Ndipo anafika woyamba, nanena, Mbuye, mina yanu inachita nionjeza mina khumi.

17 Ndipo anati kwa iye, Chabwino, kapolo wabwino iwe; popeza unakhala wokhulupirika m’chaching’onong’ono, khala nao ulamuliro pa mizinda khumi.

18 Ndipo anadza wachiwiri, nanena, Mbuye, mina yanu yapindula mina zisanu.

19 Ndipo anati kwa iyenso, Khala iwenso woweruza mizinda isanu.

20 Ndipo wina anadza, nanena, Mbuye, taonani, siyi mina yanu, ndaisunga m’kansalu;

21 pakuti ndinakuopani, popeza inu ndinu munthu wouma mtima: munyamula chimene simunachiike pansi, mututa chimene simunachifese.

22 Ananena kwa iye, Pakamwa pako ndikuweruza, kapolo woipa iwe. Unadziwa kuti ine ndine munthu wouma mtima, wonyamula chimene sindinachiike, ndi wotuta chimene sindinachifese;

23 ndipo sunapereke bwanji ndalama yanga pokongoletsa, ndipo ine pakudza ndikadaitenga ndi phindu lake?

24 Ndipo anati kwa iwo akuimirirapo, Mchotsereni minayo, nimuipatse kwa iye wakukhala nazo mina khumi.

25 Ndipo anati kwa iye, Mbuye, ali nazo mina khumi.

26 Ndinena ndi inu, kuti kwa yense wakukhala nacho kudzapatsidwa; koma kwa iye amene alibe kanthu, chingakhale chimene ali nacho chidzachotsedwa.

27 Koma adani anga aja osafuna kuti ndidzakhala mfumu yao, bwerani nao kuno, nimuwaphe pamaso panga.

28 Ndipo m’mene adanena izi anawatsogolera nakwera ku Yerusalemu.

Yesu alowa mu Yerusalemu

29 Ndipo kunali, m’mene anayandikira ku Betefage ndi Betaniya, paphiri lotchedwa la Azitona, anatuma awiri aophunzira,

30 nati, Mukani kumudzi uli pandunji panu; m’menemo, polowa, mudzapeza mwana wa bulu womangidwa, pamenepo palibe munthu anakwerapo nthawi iliyonse; mummasule iye nimumtenge.

31 Ndipo munthu akati kwa inu, Mummasuliranji? Mudzatero naye, Ambuye amfuna iye.

32 Ndipo anachoka otumidwawo, napeza monga adanena kwa iwo.

33 Ndipo pamene anamasula mwana wa bulu, eni ake anati kwa iwo, Mumasuliranji mwana wa bulu?

34 Ndipo anati, Ambuye amfuna iye.

35 Ndipo anadza naye kwa Yesu; ndipo anayalika zovala zao pa mwana wa buluyo, nakwezapo Yesu.

36 Ndipo pakupita Iye, anayala zovala zao m’njira.

37 Ndipo pakuyandikira Iye tsono potsetsereka pake paphiri la Azitona, unyinji wonse wa ophunzira anayamba kukondwera ndi kuyamika Mulungu ndi mau aakulu, chifukwa cha ntchito zonse zamphamvu anaziona;

38 nanena, Wolemekezeka Mfumuyo ikudza m’dzina la Ambuye; mtendere mu Mwamba, ndi ulemerero mu Mwambamwamba.

39 NdipoAfarisiena a m’khamu la anthu anati kwa Iye, Mphunzitsi, dzudzulani ophunzira anu.

40 Ndipo anayankha nati, Ndinena ndi inu, ngati awa khala chete miyala idzafuula.

Yesu alirira Yerusalemu

41 Ndipo m’mene anayandikira, anaona mzindawo naulirira,

42 nanena, Ukadazindikira tsiku ili, inde iwetu zinthu za mtendere! Koma tsopano zibisika pamaso pako.

43 Pakuti masiku adzakudzera, ndipo adani ako adzakuzingira linga, nadzakuzungulira iwe kwete, nadzakutsekereza ponsepo;

44 ndipo adzakupasula iwe, ndi ana ako mwa iwe; ndipo sadzasiya mwa iwe mwala wina pamwala unzake; popeza sunazindikire nyengo ya mayang’aniridwe ako.

Ayeretsa Kachisi kachiwiri

45 Ndipo analowa mu Kachisi, nayamba kutulutsa iwo akugulitsa malonda, nanena nao,

46 Kwalembedwa, Ndipo nyumba yanga idzakhala nyumba yakupemphera; koma inu mwaiyesa phanga la achifwamba.

47 Ndipo analikuphunzitsa mu Kachisi tsiku ndi tsiku. Koma ansembe aakulu, ndi alembi ndi akulu a anthu anafunafuna kumuononga Iye;

48 ndipo sanapeze chimene akachita; pakuti anthu onse anamlendewera Iye kuti amve.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/19-8a7e45abc844a3dc5a178076f8bd17a8.mp3?version_id=1068—

Categories
LUKA

LUKA 20

Amfunsa Yesu za ulamuliro

1 Ndipo kunali lina la masiku ao m’mene Iye analikuphunzitsa anthu mu Kachisi, ndi kulalikira Uthenga Wabwino, adamdzera ansembe aakulu ndi alembi pamodzi ndi akulu;

2 ndipo anati, nanena naye, Mutiuze muchita izi ndi ulamuliro wotani? Kapena ndani iye amene anakupatsani ulamuliro umene?

3 Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Ndidzakufunsani mau Inenso; mundiuze:

4 Ubatizo wa Yohane unachokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu?

5 Ndipo anatsutsana mwa okha, nanena, Ngati tinena uchokera Kumwamba; adzati, Simunamkhulupirire chifukwa ninji?

6 Ndiponso, tikanena, Uchokera kwa anthu; anthu onse adzatiponya miyala: pakuti akopeka mtima, kuti Yohane alimneneri.

7 Ndipo anayankha kuti sadziwa kumene uchokera.

8 Ndipo Yesu anati kwa iwo Ndingakhale Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndichita nao zinthu izi.

Fanizo la olima munda wampesa

9 Ndipo Iye anayamba kunena kwa anthufanizoili: Munthu analima munda wampesa, naukongoletsa kwa olima munda, nanka kudziko lina, nagonerako nthawi yaikulu.

10 Ndipo pa nyengo ya zipatso anatumiza kapolo wake kwa olima mundawo, kuti ampatseko chipatso cha mundawo; koma olimawo anampanda, nambweza wopanda kanthu.

11 Ndipo anatumizanso kapolo wina; ndipo iyenso anampanda, namchitira chipongwe, nambweza, wopanda kanthu.

12 Ndipo anatumizanso wina wachitatu; ndipo iyenso anamlasa, namtaya kunja.

13 Ndipo mwini mundawo anati, Ndidzachita chiyani? Ndidzatuma mwana wanga amene ndikondana naye; kapena akamchitira iye ulemu.

14 Koma olimawo, pamene anamuona, anauzana wina ndi mnzake, nati, Uyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe, kuti cholowa chake chikhale chathu.

15 Ndipo anamponya kunja kwa mundawo, namupha. Pamenepo mwini munda wampesawo adzawachitira chiyani?

16 Iye adzafika nadzaononga olima munda aja, nadzapatsa munda kwa ena. Ndipo pamene iwo anamva, anati, Musatero iai!

17 Koma Iye anawapenyetsa iwo, nati, Nchiyani ichi chinalembedwa,

Mwala umene anaukana omanga nyumba,

womwewu unakhala mutu wa pangodya.

18 Munthu yense wakugwa pamwala uwu, adzaphwanyika; koma iye amene udzamgwera, udzamupha.

Za msonkho

19 Ndipo alembi ndi ansembe aakulu anafunafuna kumgwira ndi manja nthawi yomweyo; ndipo anaopa anthu; pakuti anazindikira kuti ananenera pa iwo fanizo ili.

20 Ndipo anamyang’anira, natumiza ozonda, amene anadzionetsera ngati olungama mtima, kuti akamkole pa mau ake, kotero kuti akampereke Iye ku ukulu ndi ulamuliro wa kazembe.

21 Ndipo anamfunsa Iye, nanena, Mphunzitsi, ife tidziwa kuti munena ndi kuphunzitsa kolunjika, ndi kusasamalira nkhope ya munthu, koma muphunzitsa njira ya Mulungu koonadi;

22 kodi kuloledwa kupereka msonkho kwaKaisara, kapena iai?

23 Koma Iye anazindikira chinyengo chao, nati kwa iwo,

24 Tandionetsani Ine rupiya latheka. Chithunzithunzi ndi cholemba chake ncha yani? Anati iwo, Cha Kaisara.

25 Ndipo Iye anati kwa iwo, Chifukwa chake perekani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.

26 Ndipo sanakhoze kugwira mauwo pamaso pa anthu; ndipo anazizwa ndi kuyankha kwake, nakhala chete.

Yesu ayankha Asaduki za kuuka kwa akufa

27 Ndipo anadza kwa IyeAsadukiena, amene amanena kuti palibe kuuka kwa akufa; ndipo anamfunsa Iye,

28 nanena, Mphunzitsi, Mose anatilembera ife, kuti mbale wake wa munthu akafa, wokhala ndi mkazi, ndipo alibe mwana iye, mbale wake adzakwatira mkaziyo, nadzamuukitsira mbale wake mbeu.

29 Tsono panali abale asanu ndi awiri; ndipo woyamba anakwatira mkazi, nafa wopanda mwana;

30 ndipo wachiwiri,

31 ndi wachitatu anamtenga mkaziyo; ndipo choteronso asanu ndi awiri onse, sanasiye mwana, namwalira.

32 Pomalizira anamwaliranso mkaziyo.

33 Potero m’kuuka iye adzakhala mkazi wa yani wa iwo? Pakuti asanu ndi awiriwo adamkwatira iye.

34 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ana a dziko lapansi akwatira nakwatiwa:

35 koma iwo akuyesedwa oyenera kufikira dziko lijalo, ndi kuuka kwa akufa, sakwatira kapena kukwatiwa.

36 Pakuti sangathe kufanso nthawi zonse; pakuti afanafana ndiangelo; ndipo ali ana a Mulungu, popeza akhala ana a kuuka kwa akufa.

37 Koma za kuti anthu akufa auka, anasonyeza ngakhale Mose, pa Chitsamba chija, pamene iye amtchulira Ambuye, Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isaki, ndi Mulungu wa Yakobo.

38 Ndipo Iye sakhala Mulungu wa akufa, koma wa amoyo: pakuti anthu onse akhala ndi moyo kwa Iye.

39 Ndipo alembi ena anayankha nati, Mphunzitsi, mwanena bwino.

40 Pakuti sanalimbenso mtima kumfunsa Iye kanthu kena.

Khristu mwana wa Davide

41 Koma Iye anati kwa iwo, Amanena bwanji kutiKhristuyo ndiye mwana wa Davide?

42 Pakuti Davide yekha anena m’buku la Masalimo,

Ambuye ananena kwa Ambuye wanga,

ukhale padzanja langa lamanja,

43 kufikira Ine ndikaika adani ako pansi pa mapazi ako.

44 Chotero Davide anamtchula Iye Ambuye, ndipo nanga ali mwana wake bwanji?

Ophunzira achenjere nao alembi

45 Ndipo pamene anthu onse analinkumva Iye, anati kwaophunzira,

46 Chenjerani nao alembi, amene afuna kuyendayenda ovala miinjiro, nakonda kupatsidwa moni m’misika, ndi mipando yaulemu m’sunagoge, ndi malo aulemu pamaphwando;

47 amene aononga nyumba za akazi amasiye, ndipo monyenga achita mapemphero aatali; amenewo adzalandira kulanga koposa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/20-c020f66e808b62ebc37855793f1b500a.mp3?version_id=1068—

Categories
LUKA

LUKA 21

Mphatso ya mkazi wamasiye

1 Ndipo Yesu anakweza maso, naona anthu eni chuma alikuika zopereka zao mosungiramo ndalama.

2 Ndipo anaona mkazi wina wamasiye waumphawi alikuika momwemo timakobiri tiwiri.

3 Ndipo Iye anati, Zoonadi ndinena kwa inu, wamasiye uyu waumphawi anaikamo koposa onse;

4 pakuti onse amenewa anaika mwa unyinji wao pa zoperekazo; koma iye mwa kusowa kwake anaikamo za moyo wake, zonse anali nazo.

Yesu aneneratu zam’tsogolo, chiyambi cha masautso

5 Ndipo pamene ena analikunena za Kachisiyo, kuti anakonzeka ndi miyala yokoma ndi zopereka, anati Iye,

6 Zinthu izi muziona, adzafika masiku, pamenepo sudzasiyidwa pano mwala pamwala unzake, umene sudzagwetsedwa.

7 Ndipo iwo anamfunsa Iye, nati, Mphunzitsi, nanga zinthu izi zidzaoneka liti? Ndipo chizindikiro ndi chiyani pamene izi ziti zichitike?

8 Ndipo Iye anati, Yang’anirani musasocheretsedwe; pakuti ambiri adzadza m’dzina langa, nadzanena, Ndine amene; ndipo, Nthawi yayandikira; musawatsate pambuyo pao.

9 Ndipo pamene mudzamva za nkhondo ndi mapanduko, musaopsedwa; pakuti ziyenera izi ziyambe kuchitika; koma mathedwe sakhala pomwepo.

10 Pamenepo ananena nao, Mtundu wa anthu udzaukira pa mtundu wina, ndipo ufumu pa ufumu wina:

11 ndipo kudzakhala zivomezi zazikulu, ndi njala ndi miliri m’malo akutiakuti, ndipo kudzakhala zoopsa ndi zizindikiro zazikulu zakumwamba.

12 Koma zisanachitike izi, anthu adzakuthirani manja, nadzakuzunzani, nadzapereka inu ku masunagogendi ndende, nadzamuka nanu kwa mafumu ndi akazembe, chifukwa cha dzina langa.

13 Kudzakhala kwa inu ngati umboni.

14 Chifukwa chake tsimikizani mumtima mwanu, kuti usanafike mlandu musalingirire chimene mudzayankha.

15 Pakuti Ine ndidzakupatsani inu kamwa ndi nzeru, zimene adani anu onse sadzatha kuzikana kapena kuzitsutsa.

16 Koma mudzaperekedwa ngakhale ndi akukubalani, ndi abale, ndi a fuko lanu, ndi abwenzi anu; ndipo ena a inu adzakuphani.

17 Ndipo anthu onse adzadana ndi inu chifukwa cha dzina langa.

18 Ndipo silidzaonongeka tsitsi limodzi la pamutu panu.

19 Mudzakhala nao moyo wanu m’chipiriro.

Aneneratu za kupasuka kwa Yerusalemu

20 Koma pamene paliponse mudzaonaYerusalemuatazingidwa ndi magulu a ankhondo, zindikirani pamenepo kuti chipulumutso chake chayandikira.

21 Pamenepo iwo ali mu Yudeya athawire kumapiri, ndi iwo ali m’kati mwa uwo atuluke, ndi iwo ali kuminda asalowemo.

22 Chifukwa amenewa ndi masiku akubwezera, kuti zonse zidalembedwa zichitike.

23 Koma tsoka iwo akukhala ndi pakati, ndi iwo akuyamwitsa ana masiku awo! Pakuti padzakhala chisauko chachikulu padziko, ndi mkwiyo pa anthu awa.

24 Ndipo adzagwa ndi lupanga lakuthwa, nadzagwidwa ndende kunka kumitundu yonse ya anthu; ndipo mapazi a anthu akunja adzapondereza Yerusalemu kufikira kuti nthawi zao za anthu akunja zakwanira.

Za kubwera kwa Mwana wamunthu

25 Ndipo kudzakhala zizindikiro pa dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi; ndi padziko lapansi chisauko cha mitundu ya anthu, alikuthedwa nzeru pa mkokomo wake wa nyanja ndi mafunde ake;

26 anthu akukomoka ndi mantha, ndi kuyembekezera zinthu zilinkudza kudziko lapansi; pakuti mphamvu zakumwamba zidzagwedezeka.

27 Ndipo pamenepo adzaonaMwana wa Munthualinkudza mu mtambo ndi mphamvu ndi ulemerero waukulu.

28 Koma poyamba kuchitika izi weramukani, tukulani mitu yanu; chifukwa chiomboledwe chanu chayandikira.

29 Ndipo ananena naofanizo; Onani mkuyu, ndi mitengo yonse:

30 pamene iphukira, muipenya nimuzindikira pa nokha kuti dzinja lili pafupi pomwepo.

31 Inde chotero inunso, pakuona zinthu izi zilikuchitika, zindikirani kuti Ufumu wa Mulungu uli pafupi.

32 Indetu ndinena ndinu, Mbadwo uno sudzapitirira, kufikira zonse zitachitika.

33 Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.

Khalani odikira

34 Koma mudziyang’anire nokha, kuti kapena mitima yanu ingalemetsedwe ndi madyaidya ndi kuledzera, ndi zosamalira za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingafikire inu modzidzimutsa ngati msampha;

35 pakuti lidzatero ndi kufikira anthu onse akukhala pankhope padziko lonse lapansi.

36 Koma inu dikirani nyengo zonse, ndi kupemphera, kuti mukalimbike kupulumuka zonse zimene zidzachitika, ndi kuimirira pamaso pa Mwana wa Munthu.

37 Ndipo usana uliwonse Iye analikuphunzitsa mu Kachisi; ndi usiku uliwonse anatuluka, nagona paphiri lotchedwa la Azitona.

38 Ndipo anthu onse analawira mamawa kudza kwa Iye ku Kachisi kudzamvera Iye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/21-6cdd412e4786b255e8ee01d3237fd43c.mp3?version_id=1068—

Categories
LUKA

LUKA 22

Yudasi apangana kupereka Yesu

1 Ndipo chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa chinayandikira, ndicho chotchedwaPaska.

2 Ndipo ansembe aakulu ndi alembi anafunafuna maphedwe ake pakuti anaopa anthuwo.

3 NdipoSatanaanalowa mwa Yudasi wonenedwa Iskariote, amene anawerengedwa mmodzi wa khumi ndi awiriwo.

4 Ndipo iye anachoka, nalankhulana ndi ansembe aakulu ndi akazembe mompereka Iye kwa iwo.

5 Ndipo anakondwera, napangana naye kumpatsa ndalama.

6 Ndipo iye anavomera, nafunafuna nthawi yabwino yakumpereka Iye kwa iwo, pakalibe khamu la anthu.

Paska lotsiriza. Mgonero

7 Ndipo tsiku la mikate yopanda chotupitsa linafika, limene inayenera kuphedwa nsembe ya Paska.

8 Ndipo Iye anatumiza Petro ndi Yohane, nati, Pitani mutikonzere ife Paska, kuti tidye.

9 Ndipo iwo ananena naye, Mufuna tikakonzere kuti?

10 Ndipo Iye anati kwa iwo, Onani, mutalowa m’mzinda, adzakomana ndinu munthu alikusenza mtsuko wa madzi; mumtsate ameneyo kunyumba kumene akalowako iye.

11 Ndipo mukanene kwa mwini nyumbayo, Mphunzitsi anena nawe, Chipinda cha alendo chili kuti, m’mene ndikadye Paska pamodzi ndiophunziraanga?

12 Ndipo iyeyo adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokonzeka; mukakonzere kumeneko.

13 Ndipo anapita iwo, napeza monga adatero nao; ndipo anakonza Paska.

14 Ndipo itadza nthawi yake, Iye anakhala pachakudya, ndi ophunzira pamodzi ndi Iye.

15 Ndipo anati kwa iwo, Ndinalakalaka ndithu kudya Paska uwu pamodzi ndinu, ndisanayambe kusautsidwa;

16 pakuti ndinena ndi inu, sindidzadya kufikira udzakwaniridwa mu Ufumu wa Mulungu.

17 Ndipo analandira chikho, ndipo pamene adayamika, anati, Landirani ichi, muchigawane mwa inu nokha;

18 pakuti ndinena kwa inu, kuyambira tsopano Ine sindidzamwako chipatso cha mpesa, kufikira Ufumu wa Mulungu udzafika.

19 Ndipo m’mene adatenga mkate, nayamika, anaunyema, nawapatsa, nanena, Ichi ndi thupi langa lopatsidwa chifukwa cha inu; chitani ichi chikumbukiro changa.

20 Ndipo choteronso chikho, atatha mgonero, nanena, Chikho ichi ndi pangano latsopano m’mwazi wanga wothiridwa chifukwa cha inu.

21 Koma onani, dzanja lake la iye amene adzandipereka ali pagome pano pamodzi ndi Ine.

22 PakutiMwana wa Munthuamukatu, monga kunaikidwiratu; koma tsoka munthuyo amene ampereka!

23 Ndipo anayamba kufunsana mwa iwo okha, ndiye yani mwa iwo amene adzachita ichi.

Kutsutsana kwakuti wamkulu ndani?

24 Ndipo kunakhala kutsutsana mwa iwo, ndani wa iwo ayesedwe wamkulu.

25 Ndipo anati kwa iwo, Mafumu a anthu a mitundu awachitira ufumu; ndipo iwo amene awachitira ulamuliro anenedwa, Ochitira zabwino.

26 Koma sipadzatero ndi inu; komatu iye ali wamkulu mwa inu, akhale ngati wamng’ono; ndi iye ali woyamba, akhale ngati wotumikira.

27 Pakuti wamkulu ndani, iye wakuseama pachakudya kapena wakutumikirapo? Si ndiye wakuseama pachakudya kodi? Koma Ine ndili pakati pa inu monga ngati wotumikira.

28 Koma inu ndinu amene munakhala ndi Ine chikhalire m’mayesero anga;

29 ndipo Ine ndikuikirani ufumu, monganso Atate wanga anandiikira Ine, kuti mukadye ndi kumwa kugome kwanga mu Ufumu wanga;

30 ndipo mudzakhala pa mipando yachifumu ndi kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israele.

Yesu achenjeza Petro

31 Simoni, Simoni, taona, Satana anafunsa akutengeni kuti akupeteni ngati tirigu;

32 koma ndinakupempherera kuti chikhulupiriro chako chingazime; ndipo iwe, pamene watembenuka ukhazikitse abale ako.

33 Ndipo anati kwa Iye, Ambuye, ndilipo ndikapite ndi Inu kundende ndi kuimfa.

34 Ndipo Iye anati, Ndikuuza iwe, Petro, sadzalira tambala lero lino kufikira udzakana katatu kuti sundidziwa Ine.

35 Ndipo anati kwa iwo, Pamene ndinakutumizani opanda thumba la ndalama, ndi thumba la kamba, ndi nsapato, munasowa kanthu kodi? Anati iwo, Iai.

36 Ndipo anati kwa iwo, Koma tsopano, iye amene ali ndi thumba la ndalama, alitenge, ndi thumba la kamba lomwe; ndipo amene alibe, agulitse chofunda chake, nagule lupanga.

37 Pakuti ndinena ndi inu, chimene chidalembedwa chiyenera kukwanitsidwa mwa Ine, Ndipo anawerengedwa ndi anthu opanda lamulo; pakuti izi za kwa Ine zili nacho chimaliziro.

38 Ndipo iwo anati, Ambuye, taonani, malupanga awiri siwa. Ndipo anati kwa iwo, Chakwanira.

Yesu mu Getsemani

39 Ndipo Iye anatuluka, napita monga ankachitira, kuphiri la Azitona; ndi ophunzira anamtsata Iye.

40 Ndipo pofika pomwepo, anati kwa iwo, Pempherani kuti mungalowe m’kuyesedwa.

41 Ndipo anapatukana nao kutalika kwake ngati kuponya mwala, nagwada pansi napemphera,

42 nati, Atate, mukafuna Inu, chotsani chikho ichi pa Ine; koma si kufuna kwanga ai, komatu kwanu kuchitike.

43 Ndipo anamuonekera Iyemngelowa Kumwamba namlimbitsa Iye.

44 Ndipo pokhala Iye m’chipsinjo mtima anapemphera kolimba koposa ndithu: ndi thukuta lake linakhala ngati madontho aakulu a mwazi alinkugwa pansi.

45 Ndipo pamene ananyamuka pakupemphera anadza kwa ophunzira, nawapeza ali m’tulo ndi chisoni,

46 ndipo anati kwa iwo, Mugoneranji? Ukani, pempherani kuti mungalowe m’kuyesedwa.

Amgwira Yesu

47 Pamene Iye anali chilankhulire, taonani, khamu la anthu, ndipo iye wotchedwa Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anawatsogolera; nayandikira Yesu kumpsompsona Iye.

48 Koma Yesu anati kwa iye, Yudasi, ulikupereka Mwana wa Munthu ndi chimpsompsono kodi?

49 Ndipo m’mene iwo akumzinga Iye anaona chimene chiti chichitike, anati, Ambuye, tidzakantha ndi lupanga kodi?

50 Ndipo wina wa iwo anakantha kapolo wa mkulu wa ansembe, namdula khutu lake lamanja.

51 Koma Yesu anayankha nati, Lolani kufikira kumene. Ndipo anakhudza khutu lake, namchiritsa.

52 Ndipo Yesu anati kwa ansembe aakulu ndi akapitao a Kachisi, ndi akulu, amene anadza kumgwira Iye, Munatuluka ndi malupanga ndi mikunkhu kodi monga ngati kugwira wachifwamba?

53 Masiku onse, pamene ndinali ndi inu mu Kachisi, simunatanse manja anu kundigwira: koma nyengo ino ndi yanu, ndipo ulamuliro wa mdima ndi wanu.

Petro akana Yesu

54 Ndipo pamenepo anamgwira Iye, napita naye, nalowa m’nyumba ya mkulu wa ansembe. Koma Petro anatsata kutali.

55 Ndipo pamene adasonkha moto m’kati mwa bwalo, nakhala pansi pamodzi, Petro anakhala pakati pao.

56 Ndipo mdzakazi anamuona iye alikukhala m’kuwala kwake kwa moto, nampenyetsa iye, nati, Munthu uyunso anali naye.

57 Koma anakana, nati, Mkaziwe, sindimdziwa Iye.

58 Ndipo popita kamphindi, anamuona wina, nati, Iwenso uli mmodzi wa awo. Koma Petro anati, Munthu iwe, sindine.

59 Ndipo patapita ngati ora limodzi, wina ananenetsa, kuti, Zoonadi, munthu uyunso anali naye, pakuti ndiye Mgalileya

60 Koma Petro anati, Munthu iwe, sindidziwa chimene uchinena. Ndipo pomwepo, iye ali chilankhulire, tambala analira.

61 Ndipo Ambuye anapotoloka, nayang’ana Petro. Ndipo Petro anakumbukira mau a Ambuye, kuti anati kwa iye, Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.

62 Ndipo anatuluka, nalira misozi ndi kuwawa mtima.

Yesu pa bwalo la akulu a Ayuda

63 Ndipo amuna amene analikusunga Yesu anamnyoza Iye, nampanda.

64 Ndipo anamkulunga Iye m’maso, namfunsa, nati, Talota; anakupanda Iwe ndani?

65 Ndipo zambiri zina anamnenera Iye, namchitira mwano.

66 Ndipo pamene kunacha, bungwe la akulu a anthu linasonkhana, ndiwo ansembe aakulu ndi alembi; ndipo anapita naye kubwalo lao,

67 nanena, Ngati uliKhristu, utiuze. Ndipo anati kwa iwo, Ndikakuuzani, simudzavomereza;

68 ndipo ndikakufunsani kanthu, simudzayankha.

69 Koma kuyambira tsopano Mwana wa Munthu adzakhala padzanja lamanja la mphamvu ya Mulungu.

70 Ndipo onse anati, Umo mtero, muli Mwana wa Mulungu kodi? Ndipo Iye anati kwa iwo, Munena kuti ndine.

71 Ndipo iwo anati, Tifuniranjinso mboni? Pakuti ife tokha tinamva m’kamwa mwa Iye mwini.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/22-254cf6b52b058c7d14ee93ce15c297bd.mp3?version_id=1068—

Categories
LUKA

LUKA 23

Yesu pa bwalo la Pilato

1 Ndipo khamu lonselo linanyamuka kupita naye kwa Pilato.

2 Ndipo anayamba kumnenera Iye, kuti, Tinapeza munthu uyu alikupandutsa anthu a mtundu wathu, ndi kuwaletsa kupereka msonkho kwaKaisara, nadzinenera kuti Iye yekha ndiyeKhristumfumu.

3 Ndipo Pilato anamfunsa Iye, nanena, Kodi ndiwe mfumu ya Ayuda? Ndipo Iye anamyankha nati, Mwatero.

4 Ndipo Pilato anati kwa ansembe aakulu ndi makamu a anthu, Ndilibe kupeza chifukwa cha mlandu ndi munthu uyu.

5 Koma iwo anapunda kunena kuti, Amautsa anthuwo, naphunzitsa mu Yudeya yense, kuyambira ku Galileya ndi kufikira kuno komwe.

6 Koma pamene Pilato anamva, anafunsa ngati munthuyu ali Mgalileya.

7 Ndipo m’mene anadziwa kuti ali wa mu ulamuliro wake waHerode, anamtumiza Iye kwa Herode, amene anali iye mwini kuYerusalemumasiku awa.

Yesu atumidwa kwa Herode

8 Ndipo Herode, pamene anaona Yesu, anakondwa ndithu; pakuti anayamba kale kufuna kumpenya Iye, chifukwa anamva za Iye; nayembekeza kuona chizindikiro china chochitidwa ndi Iye.

9 Ndipo anamfunsa Iye mau ambiri; koma Iye sanamyankhe kanthu.

10 Ndipo ansembe aakulu ndi alembi anaimirira, namnenera Iye kolimba.

11 Ndipo Herode ndi asilikali ake anampeputsa Iye, namnyoza, namveka Iye chofunda chonyezimira, nambwezera kwa Pilato.

12 Ndipo Herode ndi Pilato anachitana chibwenzi tsiku lomwelo; pakuti kale anadana.

Yesu abwezedwa kwa Pilato. Baraba amasulidwa. Yesu amangidwa

13 Ndipo Pilato anaitana ansembe aakulu, ndi akulu, ndi anthu, asonkhane,

14 nati kwa iwo, Munadza kwa ine ndi munthu uyu ngati munthu wakupandutsa anthu: ndipo taonani, Ine ndinamfunsa za mlanduwu pamaso panu, ndipo sindinapeze pa munthuyu chifukwa cha zinthu zimene mumnenera;

15 inde, ngakhale Herode yemwe; pakuti iye anambwezera Iye kwa ife; ndipo taonani, sanachite Iye kanthu kakuyenera kufa.

16 Chifukwa chake ndidzamkwapula ndi kummasula Iye.

18 Koma iwo onse pamodzi anafuula, nati, Chotsani munthu uyu, mutimasulire Barabasi;

19 ndiye munthu anaponyedwa m’ndende chifukwa cha mpanduko m’mzinda ndi cha kupha munthu.

20 Ndipo Pilato analankhulanso nao, nafuna kumasula Yesu;

21 koma iwo anafuula, nanena, Mpachikeni, mpachikeni pamtanda.

22 Ndipo anati kwa iwo nthawi yachitatu, Nanga munthuyu anachita choipa chiyani? Sindinapeze chifukwa cha kufera Iye; chotero ndidzamkwapula Iye ndi kummasula.

23 Koma anakakamiza ndi mau okweza, napempha kuti Iye apachikidwe. Ndipo mau ao anapambana.

24 Ndipo Pilato anaweruza kuti chimene alikufunsa chichitidwe.

25 Ndipo anawamasulira amene adaponyedwa m’ndende chifukwa cha mpanduko ndi kupha munthu, amene iwo anampempha; koma anapereka Yesu mwa chifuniro chao.

Yesu panjira ya ku Gologota

26 Ndipo popita naye, anagwira munthu, Simoni wa ku Kirene, alikuchokera kuminda, namsenza iye mtanda aunyamule pambuyo pake pa Yesu.

27 Ndipo unamtsata unyinji waukulu wa anthu, ndi wa akazi amene anadziguguda pachifuwa, namlirira Iye.

28 Koma Yesu anawapotolokera nati, Ana aakazi inu a Yerusalemu, musandilirire Ine, koma mudzilirire nokha ndi ana anu.

29 Chifukwa taonani masiku alinkudza, pamene adzati, Odala ali ouma ndi mimba yosabala, ndi mawere osayamwitsa.

30 Pomwepo adzayamba kunena kwa mapiri, Igwani pa ife; ndi kwa zitunda, Bisani ife.

31 Pakuti ngati azichitira izi mtengo wauwisi, nanga kudzatani ndi wouma?

32 Ndipo analinso awiri ena, ndiwo ochita zoipa, anatengedwa pamodzi ndi Iye kuti aphedwe.

Yesu apachikidwa pamtanda

33 Ndipo pamene anafika kumalo dzina lake Bade, anampachika Iye pamtanda pomwepo, ndi ochita zoipa omwe, mmodzi kudzanja lamanja ndi wina kulamanzere.

34 Ndipo Yesu ananena, Atate, muwakhululukire iwo, pakuti sadziwa chimene achita. Ndipo anagawana zovala zake, poyesa maere.

35 Ndipo anthu anaima alikupenya. Ndi akulunso anamlalatira Iye, nanena, Anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati iye ndiye Khristu wa Mulungu, wosankhidwa wake.

36 Ndipo asilikalinso anamnyoza, nadza kwa Iye, nampatsa vinyo wosasa,

37 nanena, Ngati Iwe ndiwe mfumu ya Ayuda, udzipulumutse wekha.

38 Ndipo kunalinso lembo pamwamba pake, ndilo: UYU NDIYE MFUMU YA AYUDA.

39 Ndipo mmodzi wa ochita zoipa anapachikidwawo anamchitira Iye mwano nanena, Kodi suli Khristu Iwe? Udzipulumutse wekha ndi ife.

40 Koma winayo anayankha, namdzudzula iye, nati, Kodi suopa Mulungu, poona uli m’kulangika komweku?

41 Ndipo ifetu kuyenera; pakuti tilikulandira zoyenera zimene tinazichita: koma munthu uyu sanachite kanthu kolakwa.

42 Ndipo ananena, Yesu, ndikumbukireni m’mene mulowa Ufumu wanu.

43 Ndipo Iye ananena naye, Indetu, ndinena ndi iwe, Lero lino udzakhala ndine mu Paradaiso.

44 Ndipo ora lake pamenepo linali ngati lachisanu ndi chimodzi. Ndipo panali mdima padziko lonse kufikira ora lachisanu ndi chinai, ndipo dzuwa linada.

45 Ndipo nsalu yotchinga ya mu Kachisi inang’ambika pakati.

46 Ndipo pamene Yesu anafuula ndi mau aakulu, anati, Atate, m’manja mwanu ndipereka mzimu wanga. Ndipo pakutero anapereka mzimu wake.

47 Ndipo pamenekenturiyoanaona chinachitikacho, analemekeza Mulungu, nanena, Zoonadi munthu uyu anali wolungama.

48 Ndipo makamu onse osonkhana kudzapenya ichi, pamene anaona zinachitikazo, anapita kwao ndi kudziguguda pachifuwa.

49 Ndipo omdziwa Iye onse, ndi akazi amene adamtsata kuchokera ku Galileya, anaima kutali, naona zinthu izi.

Aika maliro a Yesu

50 Ndipo taonani, munthu dzina lake Yosefe, ndiye mkulu wa milandu, munthu wabwino ndi wolungama

51 (amene sanavomereze kuweruza kwao ndi ntchito yao) wa ku Arimatea, mudzi wa Ayuda, ndiye woyembekezera Ufumu wa Mulungu,

52 yemweyo anapita kwa Pilato napempha mtembo wake wa Yesu.

53 Ndipo anautsitsa, naukulunga m’nsalu yabafuta, nauika m’manda osemedwa m’mwala, m’menemo sanaike munthu ndi kale lonse.

54 Ndipo panali tsiku lokonzera, ndiSabatalinayandikira.

55 Ndipo akazi, amene anachokera naye ku Galileya, anatsata m’mbuyo, naona manda, ndi maikidwe a mtembo wake.

56 Ndipo anapita kwao, nakonza zonunkhira ndi mafuta abwino. Ndipo pa Sabata anapumula monga mwa lamulo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/23-5967a570e5332fcf7dc9c062d19e1e77.mp3?version_id=1068—

Categories
LUKA

LUKA 24

Yesu auka kwa akufa

1 Koma tsiku loyamba la sabata, mbandakucha, anadza kumanda atatenga zonunkhira adazikonza.

2 Ndipo anapeza mwala unakunkhunizidwa kuuchotsa pamanda.

3 Ndipo m’mene analowa sanapeze mtembo wa Ambuye Yesu.

4 Ndipo kunali, m’mene anathedwa nzeru nacho, taonani amuna awiri anaimirira pafupi pao atavala zonyezimira;

5 ndipo m’mene anakhala ndi mantha naweramira pansi nkhope zao, anati kwa iwo, Mufuniranji wamoyo pa akufa?

6 Palibe kuno Iye, komatu anauka; kumbukirani muja adalankhula nanu, pamene analinso mu Galileya,

7 ndi kunena, kuti,Mwana wa Munthuayenera kuperekedwa m’manja a anthu ochimwa, ndi kupachikidwa pamtanda, ndi kuuka tsiku lachitatu.

8 Ndipo anakumbukira mau ake,

9 nabwera kuchokera kumanda, nafotokozera zonse khumi ndi mmodziwo, ndi otsala onse omwe.

10 Koma panali Maria wa Magadala, ndi Yohana, ndi Maria amake wa Yakobo, ndi akazi ena pamodzi nao amene ananena izi kwaatumwiwo.

11 Ndipo mau awa anaoneka pamaso pao ngati nkhani zachabe, ndipo sanamvere akaziwo.

12 Koma Petro ananyamuka nathamangira kumanda, ndipo powerama anaona nsalu zabafuta pazokha; ndipo anachoka nanka kwao, nazizwa ndi chija chidachitikacho.

Zochitika panjira ya ku Emausi

13 Ndipo taonani, awiri a mwa iwo analikupita tsiku lomwelo kumudzi dzina lake Emausi, wosiyana ndiYerusalemumastadiya makumi asanu ndi limodzi.

14 Ndipo iwowa anakambirana nkhani za izi zonse zidachitika.

15 Ndipo kunali m’kukambirana kwao ndi kufunsana, Yesu mwini anayandikira, natsagana nao.

16 Koma maso ao anagwidwa kuti asamzindikire Iye.

17 Ndipo anati kwa iwo, Mau awa ndi otani mulandizanawo poyendayenda? Ndipo anaima ndi nkhope zao zachisoni.

18 Ndipo mmodzi wa iwo, dzina lake Kleopa, anayankha nati kwa Iye, Kodi iwe wekha ndiwe mlendo mu Yerusalemu ndi wosazindikira zidachitikazi masiku omwe ano?

19 Ndipo anati kwa iwo, Zinthu zanji? Ndipo anati kwa Iye, Izi za Yesu Mnazarene, ndiye munthumneneriwamphamvu m’ntchito, ndi m’mau, pamaso pa Mulungu ndi anthu onse;

20 ndi kuti ansembe aakulu ndi akulu athu anampereka Iye ku chiweruziro cha imfa, nampachika Iye pamtanda.

21 Ndipo tinayembekeza ife kuti Iye ndiye wakudzayo kudzaombola Israele. Komatunso, pamodzi ndi izi zonse lero ndilo tsiku lachitatu kuyambira zidachitika izi.

22 Komatu akazi enanso a mwa ife anatidabwitsa, ndiwo amene analawirira kumanda;

23 ndipo m’mene sanapeze mtembo wake, anadza, nanena kuti adaona m’masomphenyaangelo, amene ananena kuti ali ndi moyo Iye.

24 Ndipo ena a iwo anali nafe anachoka kunka kumanda, napeza monga momwe akazi adanena; koma Iyeyo sanamuone.

25 Ndipo Iye anati kwa iwo, Opusa inu, ndi ozengereza mtima kusakhulupirira zonse adazilankhula aneneri!

26 Kodi sanayenereKhristukumva zowawa izi, ndi kulowa ulemerero wake?

27 Ndipo anayamba kwa Mose, ndi kwa aneneri onse nawatanthauzira iwo m’malembo onse zinthu za Iye yekha.

28 Ndipo anayandikira kumudzi umene analikupitako; ndipo anachita ngati anafuna kupitirira.

29 Ndipo anamuumiriza Iye, nati, Khalani ndi ife; pakuti kuli madzulo, ndipo dzuwa lapendekatu. Ndipo analowa kukhala nao.

30 Ndipo kunali m’mene Iye anaseama nao pachakudya, anatenga mkate, naudalitsa, naunyema, napatsa iwo.

31 Ndipo maso ao anatseguka, ndipo anamzindikira Iye; ndipo anawakanganukira Iye, nawachokera.

32 Ndipo anati wina kwa mnzake, Mtima wathu sunali wotentha m’kati mwathu nanga m’mene analankhula nafe m’njira, m’mene anatitsegulira malembo?

33 Ndipo ananyamuka nthawi yomweyo nabwera ku Yerusalemu, napeza khumi ndi mmodziwo, ndi iwo anali nao atasonkhana pamodzi,

34 nanena, Ambuye anauka ndithu, naonekera kwa Simoni.

35 Ndipo iwo anawafotokozera za m’njira, ndi umo anadziwika nao m’kunyema kwa mkate.

Yesu aonekera kwa khumi ndi mmodziwo

36 Ndipo pakulankhula izi iwowa, Iye anaimirira pakati pao; nanena nao, Mtendere ukhale nanu.

37 Koma anaopsedwa ndi kuchita mantha, nayesa alikuona mzimu.

38 Ndipo anati kwa iwo, Mukhala bwanji ovutika? Ndipo matsutsano amauka bwanji m’mtima mwanu?

39 Penyani manja anga ndi mapazi anga, kuti Ine ndine mwini: ndikhudzeni, ndipo penyani; pakuti mzimu ulibe mnofu ndi mafupa, monga muona ndili nazo Ine.

40 Ndipo m’mene ananena ichi, anawaonetsera iwo manja ake ndi mapazi ake.

41 Koma pokhala iwo chikhalire osakhulupirira chifukwa cha chimwemwe, nalikuzizwa, anati kwa iwo, Muli nako kanthu kakudya kuno?

42 Ndipo anampatsa Iye chidutsu cha nsomba yokazinga.

43 Ndipo anachitenga, nachidya pamaso pao.

44 Ndipo anati kwa iwo, Awa ndi mauwo ndinalankhula nanu, paja ndinakhala ndi inu, kuti ziyenera kukwanitsidwa zonse zolembedwa za Ine m’chilamulo cha Mose, ndi aneneri, ndi Masalimo.

45 Ndipo anawatsegulira mitima yao, kuti adziwitse malembo;

46 ndipo anati kwa iwo, Kotero kwalembedwa, kuti Khristu amve zowawa, nauke kwa akufa tsiku lachitatu;

47 ndi kuti kulalikidwe m’dzina lake kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo kwa mitundu yonse, kuyambira ku Yerusalemu.

48 Inu ndinu mboni za izi.

49 Ndipo onani, Ine nditumiza pa inu lonjezano la Atate wanga; koma khalani inu m’mzinda muno, kufikira mwavekedwa ndi mphamvu yochokera Kumwamba.

Yesu akwera kunka Kumwamba

50 Ndipo anatuluka nao kufikira ku Betaniya; nakweza manja ake, nawadalitsa.

51 Ndipo kunali, pakuwadalitsa Iye analekana nao, natengedwa kunka Kumwamba.

52 Ndipo anamlambira Iye, nabwera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu;

53 ndipo anakhala chikhalire mu Kachisi, nalikuyamika Mulungu.Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/LUK/24-63d52fda51d2c9ca46d8a7457ea112f5.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE Mau Oyamba

Mau Oyamba

Mu buku la

Yohane

akumuonetsa Yesu monga Mau amuyaya a Mulungu, amene “anasandulika thupi, nakhazikika pakati pa ife.” (1.14) Monga momwe bukuli likunenera, Uthengawo unalembedwa owerenga akhulupirire kuti Yesu ndiye Khristu Mwana wa Mulungu, ndi kuti pakukhulupirira mukhale nao moyo m’dzina lake (20.31).

Atatha kunena mau oyamba amene akufanizira Yesu ndi mau osatha a Mulungu, gawo loyamba la Uthengawu likutionetsa zozizwitsa zosiyanasiyana zimene zikutitsimikizira kuti Yesu ndiye Mpulumutsi Wolonjezedwa uja, amene ali Mwana wa Mulungu. Kenaka izi zikutsatidwa ndi maneno osiyanasiyana amene akufotokoza tanthauzo la zozizwitsazo. Pa ndime zimenezi, afotokozanso kuti anthu ena anakhulupirira Yesu namutsata, pamene ena sanafune kumkhulupirira. Mutu 13 mpaka 17 anena mwachimvekere za chiyanjano chozama chimene chinalipo pakati pa Yesu ndi ophunzira ake pa usiku umene iye anagwidwa, komanso mawu achilimbikitso amene Iye anawauza asanakhomedwe pamtanda mawa lake. Mitu yotsirizira inena za kugwidwa, kuzengedwa mlandu ndi kupachikidwa pamtanda komanso kuukanso kwa Yesu, ndiponso pamene Iye anaonekera kwa ophunzira ake ataukitsidwa.

Yohane

akutsindika za mphatso ya moyo wosatha mwa Yesu, ndipo mphatso imeneyi imayamba panopa ndi kuperekedwa kwa anthu amene avomera Yesu monga njira, choonadi ndi moyo (14.6). Chinthu chimene chofunikira kwambiri mu buku la

Yohane

ndicho kufotokozera zinthu zauzimu pogwiritsidwa ntchito zinthu zimene timazidziwa masiku onse monga madzi, chakudya, kuwala, mbusa ndi nkhosa zake, mphesa ndi zipatso zake. Ndipo kuchokera pa zinthu zoonekazo, bukuli limathandiza anthu okhulupirira kuti azindikire ndi kukopeka ndi zabwino zobisika zokhudza Mulungu ndi ufumu wake.

Za mkatimu

Chiyambi 1.1-18

Yohane Mbatizi ndi ophunzira oyamba a Yesu 1.19-51

Utumiki wa Yesu 2.1—12.50

Masiku omaliza mu Yerusalemu ndi madera oyandikira 13.1—17.26

Yesu agwidwa, nazengedwa mlandu, nafa pamtanda 18.1—19.42

Yesu auka kwa akufa naonekera ophunzira ake 20.1-31

Mau otsiriza: Yesu aonekeranso ophunzira ake ku Galileya 21.1-25