Categories
MARKO

MARKO 3

Yesu achiritsa wa dzanja lopuwala

1 Ndipo analowanso m’sunagoge; ndipo munali munthu m’menemo ali ndi dzanja lake lopuwala.

2 Ndipo anamuyang’anira Iye, ngati adzamchiritsa tsiku laSabata; kuti ammange mlandu.

3 Ndipo ananena ndi munthu ali ndi dzanja lopuwala, Taimirira pakati.

4 Ndipo ananena kwa iwo, Kodi nkuloledwa tsiku la Sabata kuchita zabwino, kapena zoipa? Kupulumutsa moyo kapena kupha? Koma anakhala chete.

5 Ndipo m’mene anawaunguza ndi mkwiyo, ndi kumva chisoni chifukwa cha kuuma kwa mitima yao, ananena kwa munthuyo, Tambasula dzanja lako. Ndipo analitambasula; ndipo linachira dzanja lake.

6 NdipoAfarisianatuluka, ndipo pomwepo anamkhalira upo ndi Aherode, wakumuononga Iye.

7 Ndipo Yesu anachokako pamodzi ndiophunziraake nanka kunyanja: ndipo linamtsata khamu lalikulu la a ku Galileya, ndi a ku Yudeya,

8 ndi a kuYerusalemu, ndi a ku Idumeya, ndi a ku tsidya lina la Yordani, ndi a kufupi ku Tiro ndi Sidoni, khamu lalikulu, pakumva zazikuluzo anazichita, linadza kwa Iye.

9 Ndipo anati kwa ophunzira ake, kuti kangalawa kamlinde Iye, chifukwa cha khamulo, kuti angamkanikize Iye,

10 pakuti adawachiritsa ambiri; kotero kuti onse akukhala nazo zowawa anakanikiza Iye, kuti akamkhudze.

11 Ndipo mizimu yonyansa, m’mene inamuona Iye, inamgwadira, nifuula, niti, Inu ndinu Mwana wa Mulungu.

12 Ndipo anailimbitsira mau kuti isamuulule Iye.

Apatula ophunzira khumi ndi awiri

13 Ndipo anakwera m’phiri, nadziitanira iwo amene anawafuna Iye mwini; ndipo anadza kwa Iye.

14 Ndipo anaika khumi ndi awiri, kuti akhale ndi Iye, ndi kuti akawatume kulalikira,

15 ndi kuti akhale nao ulamuliro wakutulutsa ziwanda.

16 Ndipo Simoni anamutcha Petro;

17 ndi Yakobo mwana wa Zebedeo, ndi Yohane mbale wake wa Yakobo, iwo anawatcha Boaneje, ndiko kuti, Ana a bingu;

18 ndi Andrea, ndi Filipo, ndi Bartolomeo, ndi Mateyu, ndi Tomasi, ndi Yakobo mwana wa Alifeyo, ndi Tadeyo, ndi Simoni Mkanani,

19 ndi Yudasi Iskariote, ndiye amene anampereka Iye.

Za Yesu ndi Belezebulu

Ndipo analowa m’nyumba.

20 Ndipo anthu ambiri anasonkhananso, kotero kuti sanathe iwo konse kudya.

21 Ndipo pamene abale ake anamva, anadza kudzamgwira Iye; pakuti anati adayaluka.

22 Ndipo alembi amene adatsika ku Yerusalemu ananena kuti, Ali nayeBelezebulu, ndipo, Ndi mkulu wao wa ziwanda atulutsa ziwanda.

23 Ndipo m’mene adawaitana iwo, ananena nao m’mafanizo,Satanaangathe bwanji kutulutsa Satana?

24 Ndipo ufumu ukagawanika pa uwu wokha, sungathe kukhazikika.

25 Ndipo nyumba ikagawanika pa iyo yokha, singathe kukhazikika nyumbayo.

26 Ndipo Satana akadziukira mwini yekha, nagawanika, sangathe kukhazikika, koma atsirizika.

27 Komatu palibe munthu akhoza kulowa m’nyumba ya mwini mphamvu, ndi kufunkha akatundu ake, koma ayambe wamanga mwini mphamvuyo; ndipo pamenepo adzafunkha za m’nyumba mwake.

28 Indetu, ndinena ndi inu, Adzakhululukidwa machimo onse a ana a anthu, ndi zamwano zilizonse adzachita mwano nazo;

29 koma aliyense adzachitira Mzimu Woyera mwano alibe kukhululukidwa nthawi yonse, koma anapalamuladi tchimo losatha;

30 pakuti adanena, Ali ndi mzimu wonyansa.

Abale ake a Yesu

31 Ndipo anadza amake ndi abale ake; naima kunja, namtumira uthenga kumuitana.

32 Ndipo anthu ambiri anakhala pansi pomzinga; nanena kwa Iye, Onani, amanu ndi abale anu ali kunja akufunani Inu.

33 Ndipo anawayankha nanena, Amai wanga ndi abale anga ndani?

34 Ndipo anawaunguzaunguza iwo akumzingawo, nanena, Taonani, amai wanga ndi abale anga.

35 Pakuti aliyense achita chifuniro cha Mulungu, yemweyo ndiye mbale wanga, ndi mlongo, ndi amai.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/3-7c22451e30212b0d8e077d5bb546ab21.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 4

Fanizo la wofesa

1 Ndipo anayambanso kuphunzitsa pambali pa nyanja. Ndipo anasonkhana kwa Iye khamu lalikulukulu, kotero kuti analowa Iye mungalawa, nakhala m’nyanja; ndipo khamu lonse linakhala pamtunda m’mbali mwa nyanja.

2 Ndipo anawaphunzitsa zinthu zambiri m’mafanizo, nanena nao m’chiphunzitso chake,

3 Mverani: taonani, wofesa anatuluka kukafesa;

4 ndipo kunali, m’kufesa kwake, zina zinagwa m’mbali mwa njira, ndi mbalame zinadza ndi kuzitha kudya.

5 Ndipo zina zinagwa pa nthaka yathanthwe, pamene panalibe nthaka yambiri; ndipo pomwepo zinamera, chifukwa zinalibe nthaka yakuya;

6 ndipo litakwera dzuwa zinapserera; ndipo popeza zinalibe mizu zinakhwinyata.

7 Ndipo zina zinagwa paminga, ndipo minga inakula, nkuzitsamwitsa, ndipo sizinabale zipatso.

8 Ndipo zina zinagwa m’nthaka yabwino, ndipo zinapatsa zipatso, ndi kukula ndi kuchuluka; ndipo zinabala kupindula makumi atatu, ndi makumi asanu ndi limodzi, ndi makumi khumi.

9 Ndipo ananena, Amene ali nao makutu akumva amve.

10 Ndipo pamene anakhala pa yekha, iwo amene anali pafupi ndi Iye pamodzi ndi khumi ndi awiriwo anamfunsa za mafanizo.

11 Ndipo Iye ananena nao, Kwa inu kwapatsidwa chinsinsi cha Ufumu wa Mulungu; koma kwa iwo ali kunja zonse zichitidwa m’mafanizo;

12 kuti kupenya apenye, koma asazindikire; ndipo kumva amve, koma asadziwitse; kuti pena angatembenuke, ndi kukhululukidwa.

13 Ndipo ananena nao, Simudziwa kodi fanizo ili? Mukazindikira bwanji mafanizo onse?

Kumasulira kwa fanizo la wofesa

14 Wofesa afesa mau.

15 Ndipo iwo ndiwo a m’mbali mwa njira mofesedwamo mau; ndipo pamene anamva, pomwepo akudzaSatananachotsa mau ofesedwa mwa iwo.

16 Ndipo momwemonso iwo ndiwo amene afesedwa pathanthwe, atamva mau, awalandira pomwepo ndi kusekera;

17 ndipo alibe mizu mwa iwo okha, koma akhala kanthawi; pamenepo pakudza masautso kapena mazunzo chifukwa cha mau, pomwepo akhumudwa.

18 Ndipo ena ndiwo akufesedwa kuminga; iwo ndiwo amene adamva mau,

19 ndipo malabadiro a dziko lapansi, ndi chinyengo cha chuma, ndi kulakalaka kwa zinthu zina, zilowamo, zitsamwitsa mau, ndipo akhala opanda chipatso.

20 Ndipo iwo ofesedwa pa nthaka yabwino ndiwo oterewa akumva mau, nawalandira, nabala zipatso zakupindula makumi atatu, ndi makumi asanu ndi limodzi, ndi makumi khumi.

Fanizo la nyali

21 Ndipo ananena ndi iwo, Kodi atenga nyali kuti akaivundikire mbiya, kapena akaiike pansi pa kama, osati kuti akaiike pa choikapo chake?

22 Pakuti kulibe kanthu kobisika, koma kuti kaonetsedwe; kapena kulibe kanthu kanakhala kam’tseri, koma kuti kakaululidwe.

23 Ngati munthu ali nao makutu akumva, amve.

24 Ndipo ananena nao, Yang’anirani chimene mukumva; ndi muyeso umene muyesera nao udzayesedwa kwa inu; ndipo kudzaonjezedwa kwa inu.

25 Pakuti kwa iye amene ali nako kanthu, kadzapatsidwa; ndipo kwa iye amene alibe kanthu, kadzachotsedwa ngakhale kanthu kalikonse ali nako.

Fanizo la mbeu

26 Ndipo ananena, Ufumu wa Mulungu uli wotero, monga ngati munthu akataya mbeu panthaka;

27 nakagona ndi kuuka, usiku ndi usana, ndipo mbeu zikamera, ndi kukula, iye sadziwa umo zichitira.

28 Nthaka ibala zipatso zake yokha; uyamba mmera, zitsata ngala, pamenepo maso okhwima m’ngalamo.

29 Pakucha zipatso, pamenepo atenga chisenga, pakuti nthawi yakumweta yafika.

Fanizo la mbeu yampiru

30 Ndipo ananena, Tidzafaniziranji Ufumu wa Mulungu? Kapena tidzaulinganiza ndi fanizo lotani?

31 Ngati mbeu yampiru, imene ikafesedwa panthaka, ingakhale ichepa ndi mbeu zonse za padziko,

32 koma pamene ifesedwa, imera nkukula koposa zitsamba zonse, nkukhala ndi nthambi zazikulu; kotero kuti mbalame za m’mlengalenga zikhoza kubindikira mumthunzi mwake.

33 Ndipo ndi mafanizo otere ambiri analankhula nao mau, monga anakhoza kumva;

34 ndipo sanalankhule nao wopanda fanizo: koma m’tseri anatanthauzira zonse kwaophunziraake.

Yesu aletsa namondwe

35 Ndipo dzuwa lomwelo, pofika madzulo, ananena kwa iwo, Tiolokere tsidya lina.

36 Ndipo posiya khamulo anamtenga apite nao, monga momwe anali, mungalawa. Ndipo panali ngalawa zina pamodzi ndi Iye.

37 Ndipo panauka namondwe wamkulu wa mphepo, ndi mafunde anagavira mungalawa, motero kuti ngalawa inayamba kudzala.

38 Ndipo Iye mwini anali kutsigiro, nagona tulo pamtsamiro; ndipo anamuutsa Iye nanena kwa Iye, Mphunzitsi, kodi simusamala kuti titayika ife?

39 Ndipo anauka, nadzudzula mphepo, nati kwa nyanja, kuti, Tonthola, khala bata. Ndipo mphepo inaleka, ndipo kunagwa bata lalikulu.

40 Ndipo ananena nao, Muchitiranji mantha? Kufikira tsopano mulibe chikhulupiriro kodi?

41 Ndipo iwo anachita mantha aakulu, nanenana wina ndi mnzake, Uyu ndani nanga, kuti ingakhale mphepo ndi nyanja zimvera Iye?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/4-3e8b40ea9cc6590ef53e50c37c8f2678.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 5

Yesu achiritsa wogwidwa ndi mzimu wonyansa ku Gerasa

1 Ndipo anafika tsidya lina la nyanja, kudziko la Agerasa.

2 Ndipo pamene adatuluka mungalawa, pomwepo anakomana naye munthu wotuluka kumanda wa mzimu wonyansa,

3 amene anayesa nyumba yake kumanda; ndipo palibe munthu anakhoza kummanganso, inde ngakhale ndi unyolo;

4 pakuti ankamangidwa kawirikawiri ndi matangadza ndi maunyolo, ndipo anamwetula maunyolo, naduladula matangadza; ndipo palibe munthu anali ndi mphamvu yakumfuya.

5 Ndipo masiku onse, usiku ndi usana, anakhala m’manda ndi m’mapiri, nafuula, nadzitematema ndi miyala.

6 Ndipo pakuona Yesu kutali, anathamanga, namgwadira Iye;

7 ndipo anafuula ndi mau olimba, nanena, Ndili ndi chiyani ine ndi Inu, Yesu Mwana wa Mulungu Wamkulukulu? Ndikulumbirirani pa Mulungu, msandizunze.

8 Pakuti ananena kwa iye, Tuluka iwe, mzimu wonyansa, kwa munthuyu.

9 Ndipo anamfunsa, Dzina lako ndani? Ndipo ananena kwa Iye, Dzina langa ndine Legio; chifukwa tili ambiri.

10 Ndipo anampempha Iye kwambiri kuti asaitulutsire kunja kwake kwa dziko.

11 Ndipo panali pamenepo gulu lalikulu la nkhumba zilinkudya kuphiri.

12 Ndipo inampempha Iye, kuti, Titumizeni ife mu nkhumbazo, kuti tilowe mu izo.

13 Ndipo anailola. Ndipo mizimu yonyansa inatuluka, nilowa mu nkhumba; ndipo gulu linatsika liwiro potsetsereka ndi kulowa m’nyanja, ndizo ngati zikwi ziwiri; ndipo zinatsamwa m’nyanja.

14 Ndipo akuziweta anathawa, nauza m’mzinda, ndi kuminda. Ndipo anadza kudzaona chochitikacho.

15 Ndipo anadza kwa Yesu, napenya wogwidwa ziwandayo alikukhala pansi, wovala ndi wa nzeru zake zabwino, ndiye amene anali ndi legio; ndipo anaopa iwo.

16 Ndipo adapenyawo adawafotokozera umo anachitira ndi wogwidwa ziwandayo, ndi za nkhumbazo.

17 Ndipo anayamba kumpempha Iye kuti achoke m’malire ao.

18 Ndipo m’mene Iye analikulowa mungalawa, anampempha waziwanda uja kuti akhale ndi Iye.

19 Ndipo sanamlole, koma ananena naye, Muka kwanu kwa abale ako, nuwauze zinthu zazikulu anakuchitira Ambuye, ndi kuti anakuchitira chifundo.

20 Ndipo anamuka nayamba kulalikira ku Dekapoli zinthu zazikulu Yesu adamchitira iye; ndipo anthu onse anazizwa.

Mwana wa Yairo. Mkazi wokhudza chofunda cha Yesu

21 Ndipo pamene Yesu anaolokanso mungalawa tsidya lina, khamu lalikulu linasonkhana kwa Iye; ndipo Iye anali pambali pa nyanja.

22 Ndipo anadzako mmodzi wa akulu asunagoge, dzina lake Yairo; ndipo pakuona Iye, anagwada pa mapazi ake, nampempha kwambiri,

23 nanena, kuti, Kamwana kanga kabuthu kalinkutsirizika; ndikupemphani Inu mufikeko, muike manja anu pa iko, kuti kapulumuke, ndi kukhala ndi moyo.

24 Ndipo ananka naye pamodzi; ndipo khamu lalikulu linamtsata Iye, ndi kumkanikiza Iye.

25 Ndipo munthu wamkazi amene anali ndi nthenda yachidwalire zaka khumi ndi ziwiri,

26 ndipo anamva zowawa zambiri ndi asing’anga ambiri, nalipira zonse anali nazo osachira pang’ono ponse, koma makamaka nthenda yake idakula,

27 m’mene iye anamva mbiri yake ya Yesu, anadza m’khamu kumbuyo kwake, nakhudza chovala chake.

28 Pakuti ananena iye, Ngati ndikakhudza ngakhale zovala zake ndidzapulumutsidwa.

29 Ndipo pomwepo kasupe wa nthenda yake adaphwa; ndipo anazindikira m’thupi kuti anachiritsidwa chivutiko chake.

30 Ndipo pomwepo Yesu, pamene anazindikira mwa Iye yekha kuti mphamvu idatuluka mwa Iye, anapotoloka m’khamu, nanena, Ndani anakhudza zovala zanga?

31 Ndipoophunziraake ananena kwa Iye, Muona kuti khamu lilikukanikiza Inu, ndipo munena kodi, Wandikhudza ndani?

32 Ndipo Iye anaunguzaunguza kumuona iye amene adachita ichi.

33 Koma mkaziyo anachita mantha, ndi kunthunthumira, podziwa chimene anamchitira iye, nadza, namgwadira, namuuza choona chonse.

34 Ndipo anati kwa iye, Mwana wamkaziwe, chikhulupiriro chako chakupulumutsa; muka mumtendere, nukhale wochira chivutiko chako.

35 M’mene iye ali chilankhulire, anafika a kunyumba ya mkulu wa sunagoge, nanena, kuti, Mwana wako wafa; uvutiranjinso Mphunzitsi?

36 Koma Yesu wosasamala mau olankhulidwawo, ananena kwa mkulu wa sunagoge, Usaope, khulupirira kokha.

37 Ndipo sanalole munthu yense kutsagana naye, koma Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane mbale wake wa Yakobo.

38 Ndipo anafika kunyumba kwake kwa mkulu wa sunagoge; ndipo anaona chipiringu, ndi ochita maliro, ndi akukuwa ambiri.

39 Ndipo m’mene atalowa, ananena nao, Mubuma ndi kulira bwanji? Mwana sanafe, koma ali m’tulo.

40 Ndipo anamseka Iye pwepwete. Koma Iye anawatulutsa onse, natenga atate wa mwana, ndi amake, ndi ajawo anali naye, nalowa m’mene munali mwanayo.

41 Ndipo anagwira dzanja lake la mwana, nanena kwa iye,Talita koumi, ndiko kunena posandulika, Buthu, ndinena ndi iwe, Uka.

42 Ndipo pomwepo buthulo linauka, niliyenda; pakuti linali la zaka khumi ndi ziwiri. Ndipo anadabwa pomwepo ndi kudabwa kwakukulu.

43 Ndipo anawalamulira kwambiri kuti asadziwe ichi munthu mmodzi, nawauza kuti ampatse iye kudya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/5-b1dbb167811aa64b74cb4b84357b645d.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 6

Apeputsa Yesu ku Nazarete

1 Ndipo Iye anatuluka kumeneko; nafika kudziko la kwao; ndipoophunziraake anamtsata.

2 Ndipo pofika tsiku laSabata, anayamba kuphunzitsa m’sunagoge; ndipo ambiri anamva Iye, nazizwa, nanena, Uyu adazitenga kuti izi? Nzeru yopatsidwa kwa munthuyu njotani, ndi zamphamvu zotere zochitidwa ndi manja ake?

3 Si mmisiri wa mitengo uyu, mwana wa Maria, mbale wao wa Yakobo, ndi Yose, ndi Yudasi, ndi Simoni? Ndipo alongo ake sali nafe pano kodi? Ndipo anakhumudwa ndi Iye.

4 Ndipo Yesu ananena kwa iwo,Mnenerisakhala wopanda ulemu, koma m’dziko la kwao ndimo, ndi pakati pa abale ake, ndi m’nyumba yake.

5 Ndipo kumeneko sanakhoze Iye kuchita zamphamvu konse, koma kuti anaika manja ake pa anthu odwala owerengeka, nawachiritsa.

6 Ndipo anazizwa chifukwa cha kusakhulupirira kwao. Ndipo anayendayenda m’midzi yozungulirapo, naphunzitsa.

Yesu atuma khumi ndi awiriwo

7 Ndipo anadziitanira khumi ndi awiriwo, nayamba kuwatumiza iwo awiriawiri; nawapatsa mphamvu pa mizimu yonyansa;

8 ndipo anawauza kuti asatenge kanthu ka paulendo, koma ndodo yokha; asatenge mkate, kapena thumba, kapena ndalama m’lamba lao;

9 koma avale nsapato; ndipo anati, Musavale malaya awiri.

10 Ndipo ananena nao, Kumene kulikonse mukalowa m’nyumba, khalani komweko kufikira mukachokako.

11 Ndipo pamalo ponse sakulandirani, kapena kumvera inu, pakuchoka kumeneko, sansani fumbi lili kumapazi anu, likhale mboni ya kwa iwo.

12 Ndipo anatuluka nalalikira kuti anthu atembenuke mitima.

13 Ndipo anatulutsa ziwanda zambiri, nadzoza mafuta anthu ambiri akudwala, nawachiritsa.

Kuphedwa kwa Yohane Mbatizi

14 Ndipo mfumuHerodeanamva izi; pakuti dzina lake lidamveka; ndipo ananena, kuti, Yohane Mbatizi wauka kwa akufa, ndipo chifukwa chake mphamvu izi zichitachita mwa Iye.

15 Koma ena ananena, kuti, Ndiye Eliya. Anati enanso, Ndiye mneneri, monga ngati mmodzi wa aneneriwo.

16 Koma Herode pamene anamva, ananena, Yohane amene ndamdula mutu, wauka iyeyo.

17 Pakuti Herode, mwini yekha, adatuma anthu namgwira Yohane, nammanga m’nyumba yandende, chifukwa cha Herodiasi, mkazi wa Filipo mbale wake; chifukwa adamkwatira iye.

18 Pakuti Yohane adanena kwa Herode, Si kuloledwa kwa inu kukhala naye mkazi wa mbale wanu.

19 Ndipo Herodiasi anamuda, nafuna kumupha; koma sanakhoze;

20 pakuti Herode anaopa Yohane, podziwa kuti ali munthu wolungama ndi woyera mtima, ndipo anamsunga iye. Ndipo pamene anamva iye anathedwa nzeru, nakondwa kumva iye.

21 Ndipo pamene panafika tsiku loyenera, tsiku la kubadwa kwake kwa Herode, iye anawakonzera phwando akulu ake ndi akazembe ake ndi anthu omveka a ku Galileya;

22 ndipo pamene mwana wamkazi wa Herodiasi analowa yekha navina, anakondwetsa Herode ndi iwo akukhala naye pachakudya; ndipo mfumuyo inati kwa buthulo, Tapempha kwa ine chilichonse uchifuna, ndidzakupatsa iwe.

23 Ndipo anamlumbirira iye, kuti, Chilichonse ukandipempha ndidzakupatsa, kungakhale kukugawira ufumu wanga.

24 Ndipo anatuluka, nati kwa amake, Ndidzapempha chiyani? Ndipo iye anati, Mutu wake wa Yohane Mbatizi.

25 Ndipo pomwepo analowa m’mangum’mangu kwa mfumu, napempha kuti, Ndifuna kuti mundipatse tsopano apa, mutu wake wa Yohane Mbatizi mumbale.

26 Ndipo mfumu inamva chisoni chachikulu; koma chifukwa cha malumbiro ake, ndi cha iwo akukhala pachakudya, sanafune kumkaniza.

27 Ndipo pomwepo mfumu inatuma mnyamata, namlamulira akatenge mutu wake; ndipo iye anamuka namdula mutu m’nyumba yandende;

28 natengera mutu wake mumbale, naupereka kwa buthulo; ndipo buthu linaupereka kwa amake.

29 Ndipo m’mene ophunzira ake anamva, anadza nanyamula mtembo wake nauika m’manda.

Yesu achulukitsa mikate

30 Ndipoatumwianasonkhana kwa Yesu; namuuza zilizonse adazichita, ndi zonse adaziphunzitsa.

31 Ndipo Iye ananena nao, idzani inu nokha padera ku malo achipululu, mupumule kamphindi. Pakuti akudza ndi akuchoka anali piringupiringu, ndipo analibe nthawi yokwanira kudya.

32 Ndipo anachokera m’ngalawa kunka kumalo achipululu padera.

33 Ndipo anthu anawaona alikumuka, ndipo ambiri anawazindikira, nathamangira limodzi kumeneko pamtunda, ochokera m’midzi monse, nawapitirira.

34 Ndipo anatuluka Iye, naona khamu lalikulu la anthu, nagwidwa chifundo ndi iwo, chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mbusa; ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.

35 Ndipo pamene dzuwa lidapendeka ndithu, anadza kwa Iye ophunzira ake, nanena, Malo ano nga chipululu, ndi dzuwa lapendeka ndithu;

36 muwauze kuti amuke, alowe kuminda ndi kumidzi yozungulira, akadzigulire okha kanthu kakudya.

37 Koma Iye anayankha nati kwa iwo, Apatseni kudya ndinu. Ndipo iwo ananena naye, Kodi tikapita ife ndi kugula mikate ya pa marupiya atheka mazana awiri, ndi kuwapatsa kudya?

38 Ndipo Iye ananena nao, kuti, Muli nayo mikate ingati? Pitani, mukaone. Ndipo m’mene anadziwa ananena, Isanu, ndi nsomba ziwiri.

39 Ndipo anawalamulira kuti akhalitse pansi onse magulumagulu pamsipu.

40 Ndipo anakhala pansi mabungwemabungwe a makumi khumi, ndi a makumi asanu.

41 Ndipo Iye anatenga mikate isanuyo ndi nsomba ziwirizo nayang’ana kumwamba, nadalitsa, nagawa mikate; napatsa kwa ophunzira kuti apereke kwa iwo; ndi nsomba ziwiri anagawira onsewo.

42 Ndipo anadya iwo onse, nakhuta.

43 Ndipo anatola makombo, madengu khumi ndi iwiri, ndiponso za nsomba.

44 Ndipo amene anadya mikate iyo anali amuna zikwi zisanu.

Yesu ayenda pa nyanja

45 Ndipo pomwepo Iye anakakamiza ophunzira ake alowe m’ngalawa, ndi kumtsogolera kutsidya lija ku Betsaida, m’mene Iye yekha alimkuuza khamulo kuti amuke.

46 Ndipo atalawirana nao, anachoka Iye, nalowa m’phiri kukapemphera.

47 Ndipo pofika madzulo ngalawa inali pakati pa nyanja, ndi Iye yekha pamtunda.

48 Ndipo pakuwaona ali kuvutidwa ndi kupalasa, pakuti mphepo inadza nikomana nao, pa ulonda wachinai wa usiku Iye anadza kwa iwo, alikuyenda pamwamba pa nyanja; nati awapitirire;

49 koma iwo, pamene anamuona alikuyenda panyanja, anayesa kuti ndi mzukwa, nafuula:

50 pakuti iwo onse anamuona Iye, nanthunthumira. Koma pomwepo anawalankhula nanena nao, Limbani mtima; ndinetu, musaope.

51 Ndipo Iye anakwera, nalowa kwa iwo m’ngalawa, ndipo mphepo inaleka; ndipo anadabwa kwakukulu mwa iwo okha;

52 pakuti sanazindikire za mikateyo, koma mitima yao inauma.

53 Ndipo ataoloka iwo, anafika pamtunda ku Genesarete, nakocheza padooko.

54 Ndipo pamene anatuluka m’ngalawa anamzindikira pomwepo,

55 nathamangira dziko lonselo nayamba kunyamula anthu odwala pa mphasa zao, kufika nao kumene anamva kuti analiko Iye.

56 Ndipo kumene konse adalowa Iye m’midzi, kapena m’mizinda, kapena kumadera, anthu anagoneka odwala pamisika, nampempha Iye kuti akakhudze ngakhale mphonje yokha ya chovala chake; ndipo onse amene anamkhudza anachiritsidwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/6-44e056abd7acf338f477d9993ae47538.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 7

Miyambo ya makolo ao

1 Ndipo anasonkhana kwa IyeAfarisi, ndi alembi ena, akuchokera kuYerusalemu,

2 ndipo anaona kutiophunziraake ena anadya mkate ndi m’manja mwakuda, ndiwo osasamba.

3 Pakuti Afarisi, ndi Ayuda onse sakudya osasamba m’manja ao, kuti asungire mwambo wa akulu;

4 ndipo pakuchoka kumsika, sakudya osasamba m’thupi; ndipo zilipo zinthu zina zambiri anazilandira kuzisunga, ndizo matsukidwe a zikho, ndi miphika, ndi zotengera zamkuwa.

5 Ndipo Afarisi ndi alembi anamfunsa Iye, kuti, Bwanji ophunzira anu satsata mwambo wa akulu, koma akudya mkate wao ndi m’manja mwakuda?

6 Ndipo Iye ananena nao, Yesaya ananenera bwino za inu onyenga, monga mwalembedwa,

Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao,

koma mtima wao ukhala kutali ndi Ine.

7 Koma andilambira Ine kwachabe,

ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.

8 Musiya lamulo la Mulungu, nimusunga mwambo wa anthu.

9 Ndipo ananena nao, Bwino mukaniza lamulo la Mulungu, kuti musunge mwambo wanu.

10 Pakuti Mose anati, Lemekeza atate wako ndi amai ako; ndipo iye wakunenera zoipa atate wake kapena amai wake, afe ndithu;

11 koma inu munena, Munthu akati kwa atate wake, kapena amai wake,Korban, ndiko kuti Mtulo, chimene ukadathandizidwa nacho ndi ine,

12 simulolanso kumchitira kanthu atate wake kapena amai wake;

13 muyesa achabe mau a Mulungu mwa mwambo wanu, umene munaupereka: ndi zinthu zotere zambiri muzichita.

14 Ndipo anadziitaniranso khamu la anthu, nanena nao, Mverani Ine nonsenu, ndipo dziwitsani:

15 kulibe kanthu kunja kwa munthu kukalowa mwa iye, kangathe kumdetsa: koma zinthu zakutuluka mwa munthu, ndizo zakumdetsa munthu.

17 Ndipo m’mene Iye adalowa m’nyumba kusiyana ndi khamulo, ophunzira ake anamfunsa Iyefanizolo.

18 Ndipo ananena nao, Mutero inunso opanda nzeru kodi? Kodi simuzindikira kuti kanthu kalikonse kochokera kunja kukalowa mwa munthu, sikangathe kumdetsa iye;

19 chifukwa sikalowa mumtima mwake, koma m’mimba mwake, ndipo katulukira kuthengo? Ndipo potero anayeretsa zakudya zonse.

20 Ndipo anati, Chotuluka mwa munthu ndicho chidetsa munthu.

21 Pakuti m’kati mwake mwa mitima ya anthu, mutuluka maganizo oipa, zachiwerewere,

22 zakuba, zakupha, zachigololo, masiriro, zoipa, chinyengo, chinyanso, diso loipa, mwano, kudzikuza, kupusa:

23 zoipa izi zonse zituluka m’kati, nkudetsa munthu.

Mkazi wa Siro-Fenisiya

24 Ndipo Iye anauka nachoka kumeneko, nanka ku maiko a ku Tiro ndi Sidoni. Ndipo analowa m’nyumba, nafuna kuti asadziwe anthu; ndipo sanakhoze kubisika.

25 Koma pomwepo mkazi, kabuthu kake kanali ndi mzimu wonyansa, pamene anamva za Iye, anadza, nagwa pa mapazi ake.

26 Koma mkaziyo anali Mgriki, mtundu wake Msiro-Fenisiya. Ndipo anampempha Iye kuti atulutse chiwanda m’mwana wake.

27 Ndipo ananena naye, Baleka, ayambe akhuta ana; pakuti si kwabwino kuti titenge mkate wa ana, ndi kuutayira tiagalu.

28 Koma iye anavomera nanena ndi Iye, Inde Ambuye; tingakhale tiagalu ta pansi pa gome tikudyako nyenyeswa za ana.

29 Ndipo anati kwa iye, Chifukwa cha mau amene, muka; chiwanda chatuluka m’mwana wako wamkazi.

30 Ndipo anachoka kunka kunyumba kwake, napeza mwana atamgoneka pakama, ndi chiwanda chitatuluka.

Yesu achiritsa munthu wogontha ndi wosalankhula

31 Ndipo anatulukanso m’maiko a ku Tiro, nadzera pakati pa Sidoni, kufikira ku nyanja ya Galileya, ndi kupyola pakati pa maiko a ku Dekapoli.

32 Ndipo anadza naye kwa Iye munthu wogontha, ndi wachibwibwi; ndipo anampempha Iye kuti aike dzanja pa iye.

33 Ndipo anampatula pa khamu la anthu pa yekha, nalonga zala zake m’makutu mwake, nalavula malovu, nakhudza lilime lake:

34 nagadamira kumwamba, nausa moyo, nanena naye,Efata, ndiko, Tatseguka.

35 Ndipo makutu ake anatseguka, ndi chomangira lilime lake chinamasulidwa, ndipo analankhula chilunjikire.

36 Ndipo anawalamulira kuti asauze munthu aliyense; koma monga momwe Iye anawalamulitsa momwenso makamaka analalikira kopambana.

37 Ndipo anadabwa kwakukulukulu, nanena, Wachita Iye zonse bwino; angakhale ogontha awamvetsa, ndi osalankhula awalankhulitsa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/7-a4e70fae1048b45600f04b6543e6c177.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 8

Yesu achulukitsa mikate kachiwiri

1 Masiku ajawo pakukhalanso khamu lalikulu la anthu, ndipo analibe kanthu kakudya, Iye anadziitaniraophunziraake, nanena nao,

2 Ndimva nalo chifundo khamulo, chifukwa ali ndi Ine chikhalire masiku atatu, ndipo alibe kanthu kakudya:

3 ndipo ngati ndiwauza iwo amuke kwao osadya kanthu, adzakomoka panjira; ndipo ena a iwo achokera kutali.

4 Ndipo ophunzira ake anamyankha Iye, kuti, Munthu adzatha kutenga kuti mikate yakukhutitsa anthu awa m’chipululu muno?

5 Ndipo anawafunsa, Muli nayo mikate ingati? Ndipo anati, Isanu ndi iwiri.

6 Ndipo analamulira anthu a khamulo akhale pansi; natenga mikate isanu ndi iwiriyo, nayamika, nanyema, napatsa ophunzira ake, kuti apereke kwa iwo; ndipo anapereka kwa khamulo.

7 Ndipo anali nato tinsomba towerengeka; ndipo Iye anatidalitsa, nati atipereke itonso.

8 Ndipo anadya nakhuta; ndipo anatola makombo madengu asanu ndi awiri.

9 Ndipo iwo anali ngati zikwi zinai; ndipo Iye analawirana nao.

10 Ndipo pomwepo analowa m’ngalawa ndi ophunzira ake, nafika ku mbali ya ku Dalamanuta.

Afarisi afuna chizindikiro

11 NdipoAfarisianatuluka, nayamba kufunsana naye, ndi kufuna kwa Iye chizindikiro chochokera Kumwamba, namuyesa Iye.

12 Ndipo anausitsa moyo m’mzimu wake, nanena, Anthu a mbadwo uno afunafuna chizindikiro bwanji? Indetu ndinena kwa inu, ngati chizindikiro chidzapatsidwa kwa mbadwo uno!

13 Ndipo anawasiya iwo, nalowanso m’ngalawa, nachoka kunka ku tsidya lija.

Chotupitsa mkate cha Afarisi

14 Ndipo ophunzira adaiwala kutenga mikate, ndipo analibe mkate m’ngalawa koma umodzi wokha.

15 Ndipo Iye anawalamula, nanena, Yang’anirani, penyani kuti mupewe chotupitsa mkate cha Afarisi, ndi chotupitsa mkate chaHerode.

16 Ndipo anatsutsana wina ndi mnzake, nanena kuti, Tilibe mikate.

17 Ndipo Yesu pamene anazindikira, ananena nao, Bwanji mutsutsana chifukwa mulibe mkate? Kodi kufikira tsopano simuzindikira, nisimudziwitsa? Kodi muli nayo mitima yanu youma?

18 Pokhala nao maso simupenya kodi? Ndi pokhala nao makutu simukumva kodi? Ndipo simukumbukira kodi?

19 Pamene ndinawagawira anthu zikwi zisanu mikate isanu ija, munatola madengu angati odzala ndi makombo? Ananena naye, Khumi ndi iwiri.

20 Ndipo mikate isanu ndi iwiri kwa anthu zikwi zinai, munatola madengu angati odzala ndi makombo? Ndipo ananena naye, Asanu ndi awiri.

21 Ndipo Iye ananena nao, Simudziwitsa ngakhale tsopano kodi?

Yesu achiritsa munthu wakhungu ku Betsaida

22 Ndipo anadza ku Betsaida. Ndipo anadza naye kwa Iye munthu wakhungu, nampempha Iye kuti amkhudze.

23 Ndipo anamgwira dzanja munthu wakhunguyo, natulukira naye kunja kwa mudzi; ndipo atamthira malovu m’maso mwake, naika manja pa iye, anamfunsa, Uona kanthu kodi?

24 Ndipo anakweza maso, nanena, Ndiona anthu; pakuti ndiwapenya ayendayenda ngati mitengo.

25 Pamenepo anaikanso manja m’maso mwake; ndipo anapenyetsa, nachiritsidwa, naona zonse mbee.

26 Ndipo anamtumiza amuke kwao, nanena, Usalowe konse m’mudzi.

Petro avomereza Khristu

27 Ndipo anatuluka Yesu, ndi ophunzira ake, nalowa kumidzi ya ku Kesareya-Filipi; ndipo panjira anafunsa ophunzira ake, nanena nao, Kodi anthu ananena kuti Ine ndine yani?

28 Ndipo ananena, nati, Yohane Mbatizi; ndi ena, Eliya; koma ena, Mmodzi wa aneneri.

29 Ndipo Iye anawafunsa, Koma inu munena kuti ndine yani? Petro anayankha nanena naye, NdinuKhristu.

30 Ndipo anawauzitsa iwo kuti asanene kwa munthu mmodzi za Iye.

Yesu aneneratu za mazunzo ndi imfa yake

31 Ndipo anayamba kuwaphunzitsa, kuti kuyenera kutiMwana wa Munthuakamve zowawa zambiri, nakakanidwe ndi akulu ndi ansembe aakulu, ndi alembi, nakaphedwe, ndipo mkucha wake akauke.

32 Ndipo mauwo ananena poyera. Ndipo Petro anamtenga Iye, nayamba kumdzudzula.

33 Koma Iye anapotoloka, napenya ophunzira ake, namdzudzula Petro, nanena, Choka, pita kumbuyo kwanga,Satanaiwe; popeza susamalira zinthu za Mulungu, koma za anthu.

Kunyamula mtanda

34 Ndipo anadziitanira khamulo la anthu pamodzi ndi ophunzira ake, nati kwa iwo, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wake, nanditsate Ine.

35 Pakuti yense wakufuna kupulumutsa moyo wake adzautaya; ndipo yense wakutaya moyo wake chifukwa cha Ine, ndi chifukwa cha Uthenga Wabwino, adzaupulumutsa.

36 Pakuti munthu apindulanji akadzilemezera dziko lonse, natayapo moyo wake?

37 Pakuti munthu akapereka chiyani chosintha nacho moyo wake?

38 Pakuti yense wakuchita manyazi chifukwa cha Ine, ndi cha mau anga mu mbadwo uno wachigololo ndi wochimwa, Mwana wa Munthu adzachitanso manyazi chifukwa cha iyeyu, pamene Iye adzafika naoangeloake oyera, mu ulemerero wa Atate wake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/8-e87776aaabbc902cb1ecd2ba35a96ccc.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 9

Mawalitsidwe a Yesu paphiri

1 Ndipo ananena nao, Ndithu ndinena ndi inu kuti, Alipo ena akuimirira pano, amene sadzalawa imfa konse, kufikira akaona Ufumu wa Mulungu utadza ndi mphamvu.

2 Ndipo atapita masiku asanu ndi limodzi, Yesu anatenga Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, nakwera nao paphiri lalitali padera pa okha; ndipo anasandulika pamaso pao:

3 ndipo zovala zake zinakhala zonyezimira, zoyera mbuu; monga ngati muomba wotsuka nsalu padziko lapansi sangathe kuziyeretsai.

4 Ndipo anaonekera kwa iwo Eliya ndi Mose, alikulankhulana ndi Yesu.

5 Ndipo Petro anayankha, nanena ndi Yesu,Rabi, kutikomera ife kukhala pano; ndipo timange misasa itatu; umodzi wa inu, ndi wina wa Mose, ndi wina wa Eliya.

6 Pakuti sanadziwe chimene adzayankha; chifukwa anachita mantha ndithu.

7 Ndipo panadza mtambo wakuwaphimba iwo; ndipo mau munatuluka m’mtambomo, kuti, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa; mverani Iye.

8 Ndipo dzidzidzi pounguzaunguza, sanapenye munthu wina yense, koma Yesu yekha, ndi iwo eni.

9 Ndipo pakutsika iwo paphiri, Iye anawalamula kuti asauze munthu zinthu zimene adaziona, koma pameneMwana wa Munthuakadzauka kwa akufa.

10 Ndipo anasunga mauwo, nafunsana mwa iwo okha, kuti, Kuuka kwa akufa nchiyani?

11 Ndipo anamfunsa Iye, nanena, Nanga alembi anena kuti adzayamba kufika Eliya?

12 Ndipo Iye ananena nao, Eliya ayamba kudza ndithu, nadzakonza zinthu zonse; ndipo kwalembedwa bwanji za Mwana wa Munthu, kuti ayenera kumva zowawa zambiri ndi kuyesedwa chabe?

13 Koma ndinena ndi inu kuti anafikadi Eliya, ndipo anamchitiranso zilizonse iwo anazifuna, monga kwalembedwa za iye.

Achiritsidwa mwana wogwidwa ndi mzimu wosalankhula

14 Ndipo pamene anadza kwaophunzira, anaona khamu lalikulu la anthu ozungulira iwo, ndi alembi alikufunsana nao.

15 Ndipo pomwepo anthu onse a khamulo, pakumuona Iye, anazizwa kwambiri, namthamangira Iye, namlonjera.

16 Ndipo anawafunsa iwo, Mufunsana nao chiyani?

17 Ndipo wina wa m’khamulo anamyankha Iye, kuti, Mphunzitsi, ndadza naye kwa Inu mwana wanga, ali nao mzimu wosalankhula;

18 ndipo ponse pamene umgwira, umgwetsa; ndipo achita thovu, nakukuta mano, nanyololoka; ndipo ndinalankhula nao ophunzira anu kuti autulutse; koma sanakhoze.

19 Ndipo Iye anawayankha nanena, Mbadwo wosakhulupirira inu, ndidzakhala ndi inu kufikira liti? Ndidzakulekererani nthawi yanji? Mudze naye kwa Ine.

20 Ndipo anadza naye kwa Iye; ndipo pakumuona, pomwepo mzimuwo unamng’amba koopsa; ndipo anagwa pansi navimvinika ndi kuchita thovu.

21 Ndipo Iye anafunsa atate wake, kuti, Chimenechi chinayamba kumgwira liti? Ndipo anati, Chidamyamba akali mwana.

22 Ndipo kawirikawiri ukamtaya kumoto ndi kumadzi, kumuononga; koma ngati mukhoza kuchita kanthu mtithandize, ndi kutichitira chifundo.

23 Ndipo Yesu ananena naye, Ngati mukhoza! Zinthu zonse zitheka ndi iye wakukhulupirira.

24 Pomwepo atate wa mwana anafuula, nanena, Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga.

25 Ndipo pamene Yesu anaona kuti khamu la anthu lilikuthamangira pamodzi, anadzudzula mzimu woipawo, nanena ndi uwo, Mzimu wosalankhula ndi wogontha iwe, Ine ndikulamula iwe, tuluka mwa iye, ndipo usalowenso mwa iye.

26 Ndipo pamene unafuula, numng’ambitsa, unatuluka; ndipo mwana anakhala ngati wakufa; kotero kuti ambiri ananena, Wamwalira.

27 Koma Yesu anamgwira dzanja lake, namnyamutsa; ndipo anaimirira.

28 Ndipo pamene Iye adalowa m’nyumba, ophunzira ake anamfunsa m’tseri, kuti, Nanga bwanji sitinathe ife kuutulutsa?

29 Ndipo Iye anati kwa iwo, Mtundu uwu sungathe kutuluka ndi kanthu kena konse, koma ndi kupemphera.

Yesu anena kachiwiri za imfa yake

30 Ndipo anachoka iwo kumeneko, napyola pakati pa Galileya; ndipo Iye sanafune kuti munthu adziwe.

31 Pakuti anaphunzitsa ophunzira ake, nanena nao, kuti, Mwana wa Munthu aperekedwa m’manja anthu, ndipo adzamupha Iye; ndipo ataphedwa, adzauka pofika masiku atatu.

32 Koma iwo sanazindikire mauwo, naopa kumfunsa.

Wamkulu ndani mu Ufumu wa Mulungu?

33 Ndipo iwo anadza ku Kapernao; ndipo pamene anakhala m’nyumba, Iye anawafunsa, Munalikutsutsana ninji panjira?

34 Koma iwo anakhala chete; pakuti anatsutsana wina ndi mnzake panjira, kuti, wamkulu ndani?

35 Ndipo m’mene anakhala pansi anaitana khumi ndi awiriwo; nanena nao, Ngati munthu afuna kukhala woyamba, akhale wakuthungo wa onse, ndi mtumiki wa onse.

36 Ndipo anatenga kamwana, nakaika pakati pao, nakayangata, nanena nao,

37 Munthu aliyense adzalandira kamodzi ka tiana totere chifukwa cha dzina langa, alandira Ine; ndipo yense amene akalandira Ine, salandira Ine, koma Iye amene anandituma Ine.

Osatsutsana nafe athandizana nafe

38 Yohane anati kwa Iye, Mphunzitsi, tinaona munthu alikutulutsa ziwanda m’dzina lanu; ndipo tinamletsa, chifukwa sanalikutsata ife.

39 Koma Yesu anati, Musamamletsa iye; pakuti palibe munthu adzachita champhamvu m’dzina langa, nadzakhoza msanga kundinenera Ine zoipa.

40 Pakuti iye wosatsutsana ndi ife athandizana nafe.

41 Pakuti munthu aliyense adzakumwetsani inu chikho cha madzi m’dzina langa chifukwa muli ake aKhristu, indetu ndinena ndi inu, kuti iye sadzataya konse mphotho yake.

Malakwitso

42 Ndipo yense amene adzalakwitsa kamodzi ka tiana timeneto takukhulupirira Ine, kuli kwabwino kwa iye makamaka kuti mwala waukulu wamphero ukolowekedwe m’khosi mwake, naponyedwe iye m’nyanja.

43 Ndipo ngati dzanja lako likulakwitsa iwe, ulidule: nkwabwino kwa iwe kulowa m’moyo wopunduka dzanja, koposa kukhala ndi manja ako awiri ndi kulowa muGehena, m’moto wosazima.

45 Ndipo ngati phazi lako likulakwitsa, ulidule; kulowa iwe m’moyo wopunduka mwendo, kuli kwabwino koposa ndi kukhala ndi mapazi ako awiri ndi kuponyedwa mu Gehena.

47 Ndipo ngati diso lako likulakwitsa ulikolowole; kulowa iwe mu Ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi kuli kwabwino koposa ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu Gehena;

48 kumeneko mphutsi yao siikufa, ndi moto suzimidwa.

49 Pakuti onse adzathiridwa mchere wamoto.

50 Mchere uli wabwino; koma ngati mchere unasukuluka, mudzaukoleretsa ndi chiyani? Khalani nao mchere mwa inu nokha, ndipo khalani ndi mtendere wina ndi mnzake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/9-14eae60b02e6bfe589c82130bbb6d20a.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 10

Asasiyane mwamuna ndi mkazi wake

1 Ndipo ananyamuka Iye kumeneko, nadza ku maiko a ku Yudeya ndi ku tsidya lija la Yordani; ndipo anasonkhananso kwa Iye makamu a anthu; ndipo monga anazolowera, anawaphunzitsanso.

2 Ndipo anadza kwa IyeAfarisi, namfunsa Iye ngati kuloledwa kuti munthu achotse mkazi wake, namuyesa Iye.

3 Ndipo Iye anayankha nati kwa iwo, Kodi Mose anakulamulani chiyani?

4 Ndipo anati, Mose analola kulembera kalata yachilekaniro, ndi kumchotsa.

5 Koma Yesu anati kwa iwo, Chifukwa cha kuuma kwa mitima yanu anakulemberani lamulo ili.

6 Koma kuyambira pa chiyambi cha malengedwe anawapanga mwamuna ndi mkazi.

7 Chifukwa chake mwamuna adzasiya atate wake ndi amai wake, ndipo adzaphatikizana ndi mkazi wake;

8 ndipo awiriwa adzakhala thupi limodzi: kotero kuti salinso awiri, koma thupi limodzi.

9 Chifukwa chake chimene Mulungu anachimanga pamodzi, asachilekanitse munthu.

10 Ndipo m’nyumbaophunziraanamfunsanso za chinthu ichi.

11 Ndipo Iye ananena nao, Munthu aliyense akachotsa mkazi wake, nakakwatira wina, achita chigololo kulakwira mkaziyo;

12 ndipo ngati mkazi akachotsa mwamuna wake, nakwatiwa ndi wina, achita chigololo iyeyu.

Yesu adalitsa tiana

13 Ndipo analinkudza nato kwa Iye tiana, kuti akatikhudze; ndipo ophunzirawo anawadzudzula.

14 Koma pamene Yesu anaona anakwiya, ndipo anati kwa iwo, Lolani tiana tidze kwa Ine; musatiletse: pakuti Ufumu wa Mulungu uli wa totere.

15 Ndithu ndinena ndi inu, Munthu aliyense wosalandira Ufumu wa Mulungu ngati kamwana, sadzalowamo konse.

16 Ndipo Iye anatiyangata, natidalitsa, ndi kuika manja ake pa ito.

Mnyamata mwini chuma chambiri

17 Ndipo pamene Iye anatuluka kutsata njira, anamthamangira munthu, namgwadira Iye, namfunsa, Mphunzitsi wabwino, ndidzachita chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?

18 Ndipo Yesu anati kwa iye, Unditcha Ine wabwino bwanji? Palibe wabwino koma mmodzi, ndiye Mulungu.

19 Udziwa malamulo: Usaphe, Usachite chigololo, Usabe, Usachite umboni wakunama, Usanyenge, Lemekeza atate wako ndi amai ako.

20 Ndipo iye anati kwa Iye, Mphunzitsi, zonsezi ndinazisunga kuyambira ndili mwana.

21 Ndipo Yesu anamyang’ana, namkonda, nati kwa iye, Chinthu chimodzi chikusowa: pita, gulitsa zonse uli nazo, nuzipereke kwa anthu aumphawi, ndipo chuma udzakhala nacho m’mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

22 Koma nkhope yake inagwa pa mau awa, ndipo anachoka iye wachisoni; pakuti anali mwini chuma chambiri.

23 Ndipo Yesu anaunguzaunguza, nanena ndi ophunzira ake, Okhala nacho chuma adzalowa mu Ufumu wa Mulungu ndi kuvuta nanga!

24 Ndipo ophunzirawo anazizwa ndithu ndi mau ake. Koma Yesu anayankhanso nanena nao, Ananu, nkovuta ndithu kwa iwo akutama chuma kulowa mu Ufumu wa Mulungu!

25 Nkwa pafupi kutingamiraipyole diso la singano kuposa kuti mwini chuma alowe mu Ufumu wa Mulungu.

26 Ndipo anadabwa, nanena kwa Iye, Ndipo angathe kupulumuka ndani?

27 Yesu anawayang’ana iwo nati, Sikutheka ndi anthu, koma kutheka ndi Mulungu; pakuti zinthu zonse zitheka ndi Mulungu.

28 Petro anayamba kunena naye, Onani, ife tinasiya zonse, ndipo tinakutsatani Inu.

29 Yesu anati, Ndithu ndinena ndi inu, Palibe munthu anasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena amai, kapena atate, kapena ana, kapena minda, chifukwa cha Ine, ndi chifukwa cha Uthenga Wabwinowo,

30 amene sadzalandira makumi khumi tsopano nthawi ino, nyumba, ndi abale, ndi alongo, ndi amai, ndi ana, ndi minda, pamodzi ndi mazunzo; ndipo nthawi ilinkudza, moyo wosatha.

31 Koma ambiri akuyamba adzakhala akuthungo, ndi akuthungo adzakhala oyamba.

Ali panjira kukwera ku Yerusalemu

32 Ndipo iwo anali m’njira alinkukwera kunka ku Yerusalemu; ndipo Yesu analikuwatsogolera; ndipo iwo anazizwa; ndipo akumtsatawo anachita mantha. Ndipo Iye anatenganso khumi ndi awiriwo, nayamba kuwauza zinthu zimene zidzamfikira Iye,

33 nati, Taonani, tikwera ku Yerusalemu; ndipoMwana wa Munthuadzaperekedwa kwa ansembe aakulu ndi alembi; ndipo iwo adzamweruza kuti ayenera imfa, nadzampereka Iye kwa anthu a mitundu;

34 ndipo adzamnyoza Iye, nadzamthira malovu, nadzamkwapula Iye, nadzamupha; ndipo pofika masiku atatu adzauka.

Ana a Zebedeo apempha ulemu

35 Ndipo anadza kwa Iye Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedeo, nanena naye, Mphunzitsi, tifuna kuti mudzatichitire chimene chilichonse tidzapempha kwa Inu.

36 Ndipo Iye anati kwa iwo, Mufuna kuti ndidzakuchitireni inu chiyani?

37 Ndipo iwo anati kwa Iye, Mutipatse ife kuti tikhale mmodzi kudzanja lanu lamanja, ndi wina kulamanzere, mu ulemerero wanu.

38 Koma Yesu anati kwa iwo, Simudziwa chimene muchipempha. Mukhoza kodi kumwera chikho chimene ndimwera Ine? Kapena kubatizidwa ndi ubatizo umene ndibatizidwa nao Ine?

39 Ndipo anati kwa Iye, Tikhoza. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Chikho chimene ndimwera Ine mudzamwera; ndipo ubatizo umene ndibatizidwa nao Ine, mudzabatizidwa nao;

40 koma kukhala kudzanja langa lamanja, kapena lamanzere sikuli kwanga kupatsa; koma kuli kwa iwo amene adawakonzeratu.

41 Ndipo pamene khumiwo anamva, anayamba kupsa mtima chifukwa cha Yakobo ndi Yohane.

42 Ndipo Yesu anawaitana, nanena nao, Mudziwa kuti iwo amene ayesedwa ambuye a mitundu ya anthu amachita ufumu pa iwo; ndipo akulu ao amachita ulamuliro pa iwo.

43 Koma mwa inu sikutero ai; koma aliyense amene afuna kukhala wamkulu mwa inu adzakhala mtumiki wanu;

44 ndipo aliyense amene afuna kukhala woyamba mwa inu adzakhala kapolo wa onse.

45 Pakuti ndithu, Mwana wa Munthu sanadze kutumikiridwa, koma kutumikira, ndi kupereka moyo wake dipo la kwa anthu ambiri.

Baratimeo wakhungu wa ku Yeriko

46 Ndipo iwo anafika ku Yeriko; ndipo m’mene Iye analikutuluka mu Yeriko, ndi ophunzira ake, ndi khamu lalikulu la anthu, mwana wa Timeo, Baratimeo, wopempha wakhungu, analikukhala pansi m’mbali mwa njira.

47 Ndipo pamene anamva kuti ndi Yesu wa ku Nazarete, anayamba kufuula, ndi kunena, Yesu, Inu Mwana wa Davide, mundichitire ine chifundo.

48 Ndipo ambiri anamulamula kuti atonthole: koma makamaka anafuulitsa kuti, Inu mwana wa Davide, mundichitire chifundo.

49 Ndipo Yesu anaima, nati, Mwitaneni. Ndipo anaitana wakhunguyo, nanena naye, Limba mtima; nyamuka, akuitana.

50 Ndipo iye anataya chofunda chake, nazunzuka, nadza kwa Yesu.

51 Ndipo Yesu anamyankha, nati, Ufuna kuti ndikuchitire chiyani? Ndipo wakhunguyo anati kwa Iye, Raboni, ndilandire kuona kwanga.

52 Ndipo Yesu anati kwa iye, Muka; chikhulupiriro chako chakupulumutsa iwe. Ndipo pomwepo anapenyanso; namtsata Iye panjira.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/10-a5891fb89c35a2ecb07d1b3d2cd846cf.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 11

Yesu alowa mu Yerusalemu alikukhala pabulu

1 Ndipo pamene iwo anayandikira kuYerusalemu, ku Betefage ndi Betaniya, paphiri la Azitona, anatuma awiri aophunziraake,

2 nanena nao, Mukani, lowani m’mudzi wapandunji ndi inu; ndipo pomwepo pakulowamo mudzapeza mwana wa bulu womangidwa, amene palibe munthu anakhalapo kale lonse; mmasuleni, ndipo mubwere naye.

3 Ndipo munthu akati kwa inu, Mutero bwanji? Katini, Ambuye amfuna iye; ndipo pomwepo adzamtumiza kuno.

4 Ndipo anachoka, napeza mwana wa bulu womangidwa pakhomo, pabwalo m’khwalala, nammasula iye.

5 Ndipo ena akuima kumeneko ananena nao, Muchita chiyani ndi kumasula mwana wa bulu?

6 Ndipo anati kwa iwo monga momwe ananena Yesu: ndipo anawalola iwo apite naye.

7 Ndipo anabwera naye mwana wa bulu kwa Yesu, naika zovala zao pa iye, ndipo Iye anakhala pamenepo.

8 Ndimo ambiri anayala zovala zao panjira; ndi ena zitsamba, anazidula m’minda.

9 Ndipo akutsogolera, ndi iwo akutsata, anafuula, Hosana; Wolemekezeka Iye wakudza m’dzina la Ambuye:

10 Wolemekezeka Ufumu ulinkudza, wa atate wathu Davide; Hosana mu Kumwambamwamba.

11 Ndipo Iye analowa mu Yerusalemu, mu Kachisi; ndipo m’mene anaunguza zinthu zonse, popeza ndi madzulo, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.

Yesu atemberera mkuyu

12 Ndipo m’mawa mwake, atatuluka ku Betaniya, Iye anamva njala.

13 Ndipo anaona mkuyu kutali, uli ndi masamba; ndipo anadza Iye, kuti kapena akapezapo kanthu: ndipo m’mene anafikako anapeza palibe kanthu koma masamba okha; pakuti siinali nyengo yake ya nkhuyu.

14 Ndipo anayankha nanena ndi uwo, Munthu sadzadyanso zipatso zako nthawi zonse. Ndipo ophunzira ake anamva.

Yesu atulutsa amalonda mu Kachisi

15 Ndipo anafika iwo ku Yerusalemu; ndipo Iye analowa mu Kachisi, nayamba kutulutsa akugulitsa ndi akugula malonda mu Kachisimo, nagubuduza magome a osinthana ndalama, ndi mipando ya ogulitsa nkhunda;

16 ndipo sanalole munthu aliyense kunyamula chotengera kupyola pakati pa Kachisi.

17 Ndipo anaphunzitsa, nanena nao, Sichilembedwa kodi, Nyumba yanga idzatchedwa nyumba yakupempheramo anthu a mitundu yonse? Koma inu mwaiyesa phanga la achifwamba.

18 Ndipo ansembe aakulu ndi alembi anamva, nafunafuna momuonongera Iye; pakuti anamuopa, chifukwa khamu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.

19 Ndipo masiku onse madzulo anatuluka Iye m’mzinda.

Mkuyu wouma

20 Ndipo m’mene anapitapo m’mawa mwake, anaona kuti mkuyu uja unafota, kuyambira kumizu.

21 Ndipo Petro anakumbukira, nanena naye,Rabi, onani, wafota mkuyuwo munautemberera.

22 Ndipo Yesu anayankha nanena nao, Khulupirirani Mulungu.

23 Ndithu ndinena ndi inu, kuti, Munthu aliyense akanena ndi phiri ili, Tanyamulidwa, nuponyedwe m’nyanja; wosakayika mumtima mwake, koma adzakhulupirira kuti chimene achinena chichitidwa, adzakhala nacho.

24 Chifukwa chake ndinena ndi inu, Zinthu zilizonse mukazipemphera ndi kuzipempha, khulupirirani kuti mwazilandira, ndipo mudzakhala nazo.

25 Ndipo pamene muimirira ndi kupemphera, khululukirani, ngati munthu wakulakwirani kanthu; kuti Atate wanunso ali Kumwamba akhululukire inu zolakwa zanu.

Ubatizo wa Yohane

27 Ndipo iwo anadzanso ku Yerusalemu; ndipo m’mene Iye anali kuyenda mu Kachisi, anafika kwa Iye ansembe aakulu, ndi alembi ndi akulu;

28 nanena naye, Izi muzichita ndi ulamuliro wotani? Kapena anakupatsani ndani ulamuliro uwu wakuchita izi?

29 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ndikufunsani mau amodzi, mundiyankhe Ine, ndipo ndidzakuuzani ulamuliro umene ndichita nao zinthu zimenezi.

30 Ubatizo wa Yohane uchokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu? Mundiyankhe.

31 Ndipo anatsutsana mwa iwo okha, nanena, Tikati, Kumwamba; adzanena Iye, Ndipo simunakhulupirire iye bwanji?

32 Koma tikati, Kwa anthu, anaopa anthuwo; pakuti onse anamuyesa Yohanemnenerindithu.

33 Ndipo iwo anamyankha Yesu, ananena nao, Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndichita nao zinthu zimenezi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/11-fb491d5d1e8734a2a6fb421b36b4085d.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 12

Fanizo la osungira munda

1 Ndipo Iye anayamba kulankhula nao m’mafanizo. Munthu analima munda wampesa, nauzunguniza ndi linga, nakumba moponderamo mphesa, namanga nsanja, naukongoletsa kwa olima munda, namuka kwina.

2 Ndipo m’nyengo yake anatuma kapolo kwa olimawo, kuti alandireko kwa olimawo zipatso za m’munda wampesa.

3 Ndipo iwo anamtenga iye, nampanda, namchotsa wopanda kanthu.

4 Ndipo anatumanso kapolo wina kwa iwo; ndipo ameneyu anamlasa mutu, namchitira zomchititsa manyazi.

5 Ndipo anatuma wina; iyeyu anamupha; ndi ena ambiri; ena anawapanda, ndi ena anawapha.

6 Anamtsalira mmodzi, ndiye mwana wake wokondedwa; potsiriza anamtuma iye kwa iwo, nanena, Adzamchitira ulemu mwana wanga.

7 Koma olima ajawo, ananena mwa iwo okha, Ameneyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe iye, ndipo mundawu udzakhala wathu.

8 Ndipo anamtenga, namupha iye, namtaya kunja kwa munda.

9 Pamenepo mwini munda adzachita chiyani? Adzafika, nadzaononga olimawo, nadzapereka mundawo kwa ena.

10 Kodi simunawerenge ngakhale lembo ili,

Mwala umene anaukana omanga nyumba,

womwewu unayesedwa mutu wa pangodya:

11 Ichi chinachokera kwa Ambuye,

ndipo chili chozizwitsa m’maso mwathu?

12 Ndipo anayesa kumgwira Iye; koma anaopa khamu la anthu, pakuti anazindikira kuti Iye anakamba fanizo ili kuwatsutsa iwo; ndipo anamsiya Iye, nachoka.

Za kupereka msonkho

13 Ndipo anatuma kwa Iye ena aAfarisindi a Aherode, kuti akamkole Iye m’kulankhula kwake.

14 Ndipo pamene anafika, ananena naye, Mphunzitsi, tidziwa kuti muli woona, ndipo simusamala munthu; pakuti simuyang’ana nkhope ya anthu, koma muphunzitsa njira ya Mulungu moona: Nkuloleka kodi kupereka msonkho kwaKaisara, kapena iai?

15 Kodi tipereke kapena tisapereke? Koma Iye anadziwa chinyengo chao, nati kwa iwo, Mundiyeseranji? Nditengereni rupiya latheka, kuti ndilione. Ndipo analitenga.

16 Ndipo ananena nao, Chithunzithunzi ichi, ndi chilembo chake zili za yani? Ndipo anati kwa Iye, Za Kaisara,

17 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Perekani zake za Kaisara kwa Kaisara, ndi zake za Mulungu kwa Mulungu. Ndipo anazizwa naye kwambiri.

Asaduki afunsa za kuuka kwa akufa

18 Ndipo anadza kwa IyeAsaduki, amene amanena kuti palibe kuuka kwa akufa; ndipo anamfunsa Iye, nanena,

19 Mphunzitsi, Mose anatilembera, kuti, Akafa mbale wake wa munthu, nasiya mkazi, wosasiya mwana, mbale wake atenge mkazi wake, namuukitsire mbale wakeyo mbeu.

20 Analipo abale asanu ndi awiri; woyamba anakwatira mkazi, nafa, wosasiya mbeu;

21 ndipo wachiwiri anamkwatira, nafa, wosasiya mbeu; ndipo wachitatunso anatero momwemo;

22 ndipo asanu ndi awiriwo analibe kusiya mbeu. Potsiriza pake pa onse mkazinso anafa.

23 Pakuuka adzakhala mkazi wa yani wa iwowa? Pakuti asanu ndi awiriwo adamuyesa mkazi wao.

24 Yesu ananena nao, Simusochera nanga mwa ichi, popeza mulibe kudziwa malembo, kapena mphamvu yake ya Mulungu?

25 Pakuti pamene adzauka kwa akufa, sakwatira, kapena sakwatiwa; koma akhala ngatiangeloa Kumwamba. Koma za akufa, kuti akaukitsidwa;

26 simunawerenga m’buku la Mose kodi, za chitsambacho, kuti Mulungu anati kwa iye, nanena, Ine Ndine Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isaki, ndi Mulungu wa Yakobo?

27 Sali Mulungu wa akufa, koma wa amoyo: musochera inu ndithu.

Lamulo loposa onse

28 Ndipo anadza mmodzi wa alembi, namva iwo alikufunsana pamodzi, ndipo pakudziwa kuti anawayankha bwino, anamfunsa Iye, Lamulo la m’tsogolo la onse ndi liti?

29 Yesu anayankha, kuti, La m’tsogolo ndili, Mvera, Israele; Ambuye Mulungu wathu, Ambuye ndiye mmodzi;

30 ndipo uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mphamvu yako yonse.

31 Lachiwiri ndi ili, Uzikonda mnzako monga udzikonda mwini. Palibe lamulo lina lakuposa awa.

32 Ndipo mlembiyo anati kwa Iye, Chabwino, Mphunzitsi, mwanena zoona kuti ndiye mmodzi; ndipo palibe wina, koma Iye:

33 ndipo, kumkonda Iye ndi mtima wonse, ndi nzeru yonse, ndi mphamvu yonse, ndi kukonda mnzake monga adzikonda mwini, ndiko kuposa nsembe zopsereza zamphumphu zonse, ndi nsembe zophedwa.

34 Ndipo pakuona kuti anayankha ndi nzeru, Yesu anati kwa iye, Suli kutali ndi Ufumu wa Mulungu. Ndipo palibe munthu analimbanso mtima kumfunsa Iye kanthu.

Khristu mwana wa Davide

35 Ndipo Yesu pamene anaphunzitsa mu Kachisi, anayankha, nanena, Bwanji alembi anena kutiKhristundiye mwana wa Davide?

36 Davide mwini yekha anati mwa Mzimu Woyera, Ambuye anati kwa Ambuye wanga, Khala kudzanja langa lamanja, kufikira ndiwaika adani ako popondapo mapazi ako.

37 Davide mwini yekha amtchula Iye Ambuye; ndipo ali mwana wake bwanji? Ndipo anthu a makamuwo anakondwa kumva Iye.

Yesu awachenjeza za Alembi

38 Ndipo m’chiphunzitso chake ananena, Yang’anirani mupewe alembi, akufuna kuyendayenda ovala miinjiro, ndi kulonjeredwa pamisika,

39 ndi kukhala nayo mipando yaulemu m’sunagoge, ndi malo aulemu pamaphwando:

40 amenewo alusira nyumba za akazi amasiye, napemphera monyenga mau ambiri; amenewa adzalandira kulanga koposa.

Mphatso ya mkazi wamasiye

41 Ndipo Iye anakhala pansi pandunji pa mosungiramo ndalama, napenya kuti khamu la anthu alikuponya ndalama mosungiramo; ndipo eni chuma ambiri anaponyamo zambiri.

42 Ndipo anadza mkazi wamasiye waumphawi, ndipo iye anaponyamo tindalama tiwiri tating’ono tokwanira kakobiri kamodzi.

43 Ndipo anaitanaophunziraake, nati kwa iwo, Ndithu ndinena ndi inu, Mkazi wamasiye amene waumphawi anaponya zambiri koposa onse akuponya mosungiramo:

44 pakuti anaponyamo onse mwa zochuluka zao; koma iye anaponya mwa kusowa kwake zonse anali nazo, inde moyo wake wonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/12-49808ba024d1d004e935a63d8de06d00.mp3?version_id=1068—