Categories
ZEKARIYA

ZEKARIYA 10

Malonjezo a kwa Israele

1 Pemphani kwa Yehova mvula, m’nyengo ya mvula ya masika, kwa Yehova wolenga mphezi; ndipo adzawapatsa mivumbi ya mvula, kwa yense zophukira kuthengo.

2 Pakutiaterafianena zopanda pake, ndi aula aona bodza; nafotokoza maloto achabe, asangalatsa nazo zopanda pake; chifukwa chake ayendayenda ngati nkhosa, azunzika popeza palibe mbusa.

3 Mkwiyo wanga wayakira abusa, ndipo ndidzalanga atonde; pakuti Yehova wa makamu adzazonda zoweta zake, ndizo nyumba ya Yuda, nadzaziika ngati kavalo wake waulemerero kunkhondo.

4 Kwa iye kudzafuma mwala wa kungodya, kwa iye msomali, kwa iye uta wankhondo, kwa iye osautsa onse pamodzi.

5 Ndipo adzakhala ngati ngwazi zakupondereza adani m’thope la kubwalo kunkhondo; ndipo adzachita nkhondo, chifukwa Yehova ali nao; ndi apakavalo adzachitidwa manyazi.

6 Ndipo ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda, ndi kusunga nyumba ya Yosefe, ndipo ndidzawakhalitsa, pakuti ndawachitira chifundo; ndipo adzakhala monga ngati sindinawataye konse; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wao, ndipo ndidzawamvera.

7 Ndipo iwo a ku Efuremu adzakhala ngati ngwazi, ndi mtima wao udzakondwera ngati ndi vinyo; ndipo ana ao adzachiona nadzakondwera; mtima wao udzakondwerera mwa Yehova.

8 Ndidzawaimbira mluzu ndi kuwasonkhanitsa, pakuti ndawaombola; ndipo adzachuluka monga anachulukira kale.

9 Ndipo ndidzawafesa mwa mitundu ya anthu, ndipo adzandikumbukira m’maiko akutali; nadzakhala pamodzi ndi ana ao, nadzabwera.

10 Ndidzawatenganso kudziko la Ejipito, ndi kuwasonkhanitsa mu Asiriya; ndipo ndidzalowa nao m’dziko la Giliyadi ndi Lebanoni; koma sadzawafikira.

11 Ndipo adzapita pakati pa nyanja ya nsautso, nadzapanda mafunde a m’nyanja, ndi maiwe onse a mtsinje adzaphwa; ndi kudzikuza kwa Asiriya kudzagwetsedwa; ndi ndodo yachifumu ya Ejipito idzachoka.

12 Ndipo ndidzawalimbitsa mwa Yehova; ndipo adzayendayenda m’dzina lake; ati Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ZEC/10-503331c6c85d45c22e6c740027a12733.mp3?version_id=1068—

Categories
ZEKARIYA

ZEKARIYA 11

Kulangidwa kwa osalapa

1 Tsegula pa makomo ako Lebanoni, kuti moto uthe mikungudza yako.

2 Chema, mtengo wamlombwa, pakuti mkungudza wagwa, popeza mitengo yokoma yaipitsidwa; chemani athundu a ku Basani, pakuti nkhalango yotchinjirizika yagwa pansi.

3 Mau a kuchema kwa abusa! Pakuti ulemerero wao waipsidwa; mau a kubangula kwa misona ya mikango! Pakuti kudzikuza kwa Yordani kwaipsidwa.

4 Atero Yehova Mulungu wanga: Dyetsani zoweta zakukaphedwa;

5 zimene eni ake azipha, nadziyesera osapalamula; ndi iwo akuwagulitsa akuti, Alemekezedwe Yehova, pakuti ine ndine wolemera; ndi abusa ao sazichitira chifundo.

6 Pakuti sindidzachitiranso chifundo okhala m’dzikomo, ati Yehova; koma taonani, ndidzapereka anthu, yense m’dzanja la mnansi wake, ndi m’dzanja la mfumu yake; ndipo iwo adzakantha dzikoli, ndi m’dzanja mwao sindidzawalanditsa.

7 M’mwemo ndinadyetsa zoweta zakukaphedwa, ndizo zoweta zonyankhalala. Ndipo ndinadzitengera ndodo ziwiri; ina ndinaitcha Chisomo, inzake ndinaitcha Chomanganitsa; ndipo ndinadyetsa zowetazo.

8 Ndipo ndinatha abusa atatuwo mwezi umodzi; pakuti mtima wanga unalema nao, ndi mtima waonso unaipidwa nane.

9 Pamenepo ndinati, Sindidzadyetsanso inu; chilikufa chife; chosoweka chisoweke; ndi zotsala zidyane, chonse nyama ya chinzake.

10 Ndipo ndinatenga ndodo yanga Chisomo, ndi kuidula pakati, kuti ndiphwanye pangano langa ndinalichita ndi mitundu yonse ya anthu.

11 Ndipo linathyoka tsikulo, momwemo zonyankhalala za zoweta, zakundisamalira Ine, zinadziwa kuti ndiwo mau a Yehova.

12 Ndipo ndinanena nao, Chikakomera inu, ndipatseni mphotho yanga; ngati iai, lekani. Ndipo anayesa mphotho yanga, kulemera kwake masekeli asilivamakumi atatu.

13 Ndipo Yehova anati kwa ine, Kaziponye kwa woumba mbiya, mtengo wake wokometsetsa anandiyesawo. Ndipo ndinatenga masekeli makumi atatu a siliva, ndi kuziponya kwa woumba mbiya, m’nyumba ya Yehova.

14 Pamenepo ndinadula ndodo yanga ina, ndiyo Chomanganitsa, kuti ndithetse chibale cha pakati pa Yuda ndi Israele.

15 Ndipo Yehova anati kwa ine, Dzitengerenso zipangizo za mbusa wopusa.

16 Pakuti taonani, ndidzautsa mbusa m’dziko amene sadzazonda otayika, kapena kufunafuna zomwazika, kapena kulunzitsa yothyoka, kapena kudyetsa yamoyo, koma adzadya nyama ya zonenepa, nadzang’amba ziboda zao.

17 Tsoka mbusa wopanda pake, wakusiya zoweta! Lupanga padzanja lake, ndi pa diso lake la kumanja; dzanja lake lidzauma konse, ndi diso lake lamanja lidzada bii.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ZEC/11-c561b50ce92666c22592fbac7470bb2b.mp3?version_id=1068—

Categories
ZEKARIYA

ZEKARIYA 12

Ukulu wa Israele m’tsogolo

1 Katundu wa mau a Yehova wakunena Israele.

Atero Yehova, wakuyala miyamba, ndi kuika maziko a dziko lapansi, ndi kulenga mzimu wa munthu m’kati mwake;

2 Taonani, ndidzaikaYerusalemuakhale chipanda chodzandiritsa kwa mitundu yonse ya anthu yozungulirapo, ndipo chidzafikira Yuda yemwe pomangira misasa Yerusalemu.

3 Ndipo kudzachitika tsiku ilo, ndidzaika Yerusalemu akhale mwala wolemetsa mitundu yonse ya anthu; onse akuusenza adzadzilasa nao; ndiamitunduonse a padziko lapansi adzasonkhana kutsutsana nao.

4 Tsiku ilo, ati Yehova, ndidzakantha kavalo aliyense ndi kumdabwitsa, ndi womkwera adzayaluka; ndipo ndidzatsegulira maso anga nyumba ya Yuda, ndi kukantha kavalo aliyense wa mitundu ya anthu akhale wakhungu.

5 Ndipo akalonga a Yuda adzanena m’mtima mwao, Okhala mu Yerusalemu ndiwo mphamvu yanga mu Yehova wa makamu Mulungu wao.

6 Tsiku ilo ndidzaika akalonga a Yuda ngati phale la moto pansi pa nkhuni, ndi ngati muuni wamoto mwa mitolo ya tirigu; ndipo adzatha mitundu yonse ya anthu pozungulirapo, kudzanja lamanja ndi lamanzere; ndipo Yerusalemu adzakhalanso m’malo mwake, mu Yerusalemu.

7 Ndipo Yehova adzayamba kupulumutsa mahema a Yuda, kuti ulemerero wa nyumba ya Davide ndi ulemerero wa okhala mu Yerusalemu usakulire Yuda.

8 Tsiku ilo Yehova adzatchinjiriza okhala mu Yerusalemu; ndi iye wokhumudwa pakati pao tsiku lomwelo adzakhala ngati Davide; ndi nyumba ya Davide idzakhala ngati Mulungu, ngati mthenga wa Yehova pakati pao.

9 Ndipo kudzachitika tsiku lomwelo, ndidzayesa kuononga amitundu onse akudza kuyambana ndi Yerusalemu.

10 Ndipo ndidzatsanulira pa nyumba ya Davide, ndi pa okhala mu Yerusalemu, mzimu wa chisomo ndi wakupembedza; ndipo adzandipenyera Ine amene anandipyoza; nadzamlira ngati munthu alira mwana wake mmodzi yekha, nadzammvera zowawa mtima, monga munthu amvera zowawa mtima mwana wake woyamba.

11 Tsiku lomwelo kudzakhala maliro aakulu mu Yerusalemu, ngati maliro a Hadadirimoni m’chigwa cha Megido.

12 Ndipo dziko lidzalira, banja lililonse pa lokha; banja la nyumba ya Davide pa lokha, ndi akazi ao pa okha; banja la nyumba ya Natani pa lokha, ndi akazi ao pa okha;

13 banja la nyumba ya Levi pa lokha, ndi akazi ao pa lokha; banja la Asimei pa okha, ndi akazi ao pa okha;

14 mabanja onse otsala, banja lililonse pa lokha, ndi akazi ao pa okha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ZEC/12-2118067be46e224f9ad6caa6e917a36b.mp3?version_id=1068—

Categories
ZEKARIYA

ZEKARIYA 13

Kuyeretsedwa kwa Yerusalemu

1 Tsiku lomwelo padzatsegukira nyumba ya Davide ndi okhala muYerusalemukasupe wa kwa uchimo ndi chidetso.

2 Ndipo kudzachitika tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu, ndidzaononga maina a mafano m’dziko; ndipo sadzakumbukikanso; ndipo ndidzachotsa m’dziko aneneri ndi mzimu wachidetso.

3 Ndipo kudzachitika, akaneneranso wina, atate wake ndi mai wake ombala adzanena naye, Sudzakhala ndi moyo, pakuti unena bodza m’dzina la Yehova; ndipo atate wake ndi mai wake ombala adzamgwaza ponenera iye.

4 Ndipo kudzachitika tsiku lomwelo kuti aneneri adzachita manyazi yense ndi masomphenya ake, ponenera iye; ndipo sadzavala chofunda chaubweya kunyenga nacho;

5 koma adzati, Sindilimneneri, ndili wolima munda; pakuti munthu anandiyesa kapolo kuyambira ubwana wanga.

6 Ndipo wina akati kwa iye, Zipsera izi m’manja mwako nza chiyani? Adzayankha, Ndizo za mabala anandilasa m’nyumba ya ondikonda.

7 Galamuka, lupanga, pa mbusa wanga, ndi pa munthu mnzanga wa pamtima, ati Yehova wa makamu; kantha mbusa, ndi nkhosa zidzabalalika; koma ndidzabwezera dzanja langa pa zazing’onozo.

8 Ndipo kudzachitika m’dziko lonse, ati Yehova, magawo awiri m’menemo adzalikhidwa nadzafa; koma gawo lachitatu lidzasiyidwa m’mwemo.

9 Ndi gawo lachitatulo ndidzalitengera kumoto, ndi kuwayenga ngati ayengasiliva, ndi kuwayesa monga ayesa golide; adzaitana dzina langa, ndipo ndidzawamvera; ndidzati, Awa ndi anthu anga; ndi iwo adzati, Yehova ndi Mulungu wanga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ZEC/13-a48dca69451c712359d3cb13edf5c628.mp3?version_id=1068—

Categories
ZEKARIYA

ZEKARIYA 14

Yehova adzathandiza a ku Yerusalemu polimbana ndi amitundu

1 Taonani likudza tsiku la Yehova, limene zofunkha zako zidzagawanika pakati pako.

2 Pakuti ndidzasonkhanitsa amitundu onse alimbane ndiYerusalemu; ndipo mzindawo udzalandidwa, ndi nyumba zidzafunkhidwa, ndi akazi adzakakamizidwa; ndi limodzi la magawo awiri la mzinda lidzatuluka kunka kundende, koma anthu otsala sadzaonongeka m’mzindamo.

3 Pamenepo Yehova adzatuluka, nadzachita nkhondo ndi amitundu aja, monga anachitira nkhondo tsiku lakudumana.

4 Ndi mapazi ake adzaponda tsiku lomwelo paphiri la Azitona, lili pandunji pa Yerusalemu kum’mawa, ndi phiri la Azitona lidzang’ambika pakati kuloza kum’mawa ndi kumadzulo, ndipo padzakhala chigwa chachikulu; ndi gawo lina la phirilo lidzamuka kumpoto, ndi gawo lina kumwera.

5 Pamenepo mudzathawa kudzera chigwa cha mapiri anga; pakuti chigwa cha mapiri chidzafikira ku Azali; ndipo mudzathawa monga umo munathawira chivomezi, masiku a Uziya mfumu ya Yuda; ndipo Yehova Mulungu wanga adzadza, ndi opatulika onse pamodzi ndi Inu.

6 Ndipo kudzachitika tsiku lomwelo, sikudzakhala kuunika, zowalazo zidzada;

7 koma lidzakhala tsiku la pa lokha lodziwika ndi Yehova; palibe usana, palibe usiku; koma kudzatero kuti madzulo kudzati mbee.

8 Ndipo kudzachitika tsiku lomwelo kuti madzi amoyo adzatuluka ku Yerusalemu; gawo lao lina kunka ku nyanja ya kum’mawa, ndi gawo lina kunka ku nyanja ya kumadzulo; adzatero nyengo ya dzinja ndi ya mwamvu.

Yehova mfumu ya dziko lonse lapansi

9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu ya dziko lonse; tsiku lomwelo Yehova adzakhala Iye yekha, ndi dzina lake ilo lokha.

10 Dziko lonse lidzasandulika, lidzanga chidikha, kuyambira ku Geba kufikira ku Rimoni, kumwera kwa Yerusalemu; ndipo pali uwupo padzakhala ponyamuka, ndipo udzakhala m’malo mwake, kuyambira ku Chipata cha Benjamini kufikira ku malo a chipata choyamba, kufikira ku Chipata cha Kungodya, ndi kuyambira Nsanja ya Hananele kufikira ku zoponderamo mphesa za mfumu.

11 Ndipo anthu adzakhala m’menemo, ndipo sipadzakhalanso kuonongetsa; koma Yerusalemu adzakhala mosatekeseka.

12 Ndipo mliri umene Yehova adzakantha nao mitundu yonse ya anthu imene idathira nkhondo pa Yerusalemu ndi uwu: nyama yao idzaonda akali chilili pa mapazi ao, ndi maso ao adzapuwala m’funkha mwao, ndi lilime lao lidzanyala m’kamwa mwao.

13 Ndipo kudzali tsiku lomwelo, kuti chisokonezo chachikulu chochokera kwa Yehova chidzakhala pakati pao; ndipo adzagwira yense dzanja la mnzake; ndi dzanja lake lidzaukira dzanja la mnzake.

14 Ndi Yuda yemwe adzachita nkhondo ku Yerusalemu; ndi zolemera za amitundu onse ozungulirapo zidzasonkhanitsidwa, golide, ndisiliva, ndi zovala zambirimbiri.

15 Momwemonso mliri wa pa akavalo, nyuru,ngamira, ndi abulu, ndi nyama zonse zokhala m’misasa iyo, udzakhala ngati mliri uwo.

16 Ndipo kudzachitika kuti otsala onse a amitundu onse anadzawo kulimbana ndi Yerusalemu, adzakwera chaka ndi chaka kulambira mfumu Yehova wa makamu, ndi kusungachikondwerero cha Misasa.

17 Ndipo kudzachitika kuti aliyense wa mabanja a dziko wosakwera kunka ku Yerusalemu kulambira mfumu Yehova wa makamu, pa iwowa sipadzakhala mvula.

18 Ndipo banja la ku Ejipito likapanda kukwera, losafika, sudzawagwera kodi mliri umene Yehova adzakantha nao amitundu osakwera kusunga chikondwerero cha Misasa?

19 Ili ndi tchimo la Ejipito, ndi tchimo la amitundu onse osakwerako kusunga chikondwerero cha Misasa.

20 Tsiku lomwelo padzaoneka pa miliu ya akavalo Opatulikira Yehova; ndi mbiya za m’nyumba ya Yehova zidzanga mbale za kuguwa la nsembe.

21 Inde mbiya zonse za mu Yerusalemu ndi mu Yuda zidzakhala zopatulikira Yehova wa makamu; ndi onse akuphera nsembe adzafika nadzatengako, ndi kuphikamo; ndipo tsiku lomwelo simudzakhalanso Mkanani m’nyumba ya Yehova wa makamu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ZEC/14-53a0f47735b45fc9f2b90c20be8958b5.mp3?version_id=1068—