Categories
YONA

YONA Mau Oyamba

Mau Oyamba

Buku la

Yona

likusiyana ndi mabuku ena a aneneri a mu Baibulo chifukwa likufotokoza mwatsatanetsatane zimene adachita mneneriyo amene sadafune kumvera lamulo la Mulungu. Mulungu anamuuza kuti apite kumzinda wa Ninive, umene unali likulu ka ufumu wamphamvu wa Asiriya, amene anali mdani woipitsitsa wa Aisraele. Koma Yona sanafune kukalalikira uthenga wa Mulungu kumeneko, chifukwa amakhulupirira kuti Mulunguyo sakaononga mzindawo. Patachitika zinthu zingapo zodabwitsa, iyeyo anavomera ndipo pa mapeto ake anakwiya ataona kuti uthenga wake wa chilango sunapherezere.

Bukuli likuonetsa kuti Mulungu ali ndi ulamuliro wonse pa chilengedwe. Komanso likuonetsa kuti Mulungu ndi wachikondi ndi wachifundo, amene amafunitsitsa kukhululukira ndi kupulumutsa adani a anthu ake ngati alapa, osati ndi kuwalanga kapena kuwaononga.

Za mkatimu

Kuitanidwa kwa Yona ndi kusamvera kwake

1.1-17

Yona alapa napulumutsidwa

2.1-10

Uthenga wa Yona wotsutsana ndi Ninive

3.1-10

Chifundo cha Mulungu pa Ninive

4.1-11

Categories
YONA

YONA 1

Kuitanidwa kwa Yona, kuthawa kwake, ndi kulangidwa kwake

1 Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yona mwana wa Amitai, ndi kuti,

2 Nyamuka, pita ku Ninive, mzinda waukuluwo, nulalikire motsutsana nao; pakuti choipa chao chandikwerera pamaso panga.

3 Koma Yona ananyamuka kuti athawire ku Tarisisi, kuzemba Yehova; ndipo anatsikira ku Yopa, napezako chombo chomuka ku Tarisisi, napereka ndalama zake, natsikira m’menemo, kuti apite nao ku Tarisisi kuzemba Yehova.

4 Koma Yehova anautsa chimphepo chachikulu panyanja, ndipo panali namondwe wamkulu panyanja, ndi chombo chikadasweka.

5 Pamenepo amalinyero anachita mantha, nafuulira yense kwa mulungu wake, naponya m’nyanja akatundu anali m’chombo kuchipepuza. Koma Yona adatsikira m’munsi mwa chombo, nagona tulo tofa nato.

6 Ndipo mwini chombo anadza kwa iye, nanena naye, Utani iwe wam’tulo? Uka, itana Mulungu wako, kapena Mulunguyo adzatikumbukira tingatayike.

7 Ndipo anati yense kwa mnzake, Tiyeni tichite maere, kuti tidziwe choipa ichi chatigwera chifukwa cha yani. M’mwemo anachita maere, ndipo maere anagwera Yona.

8 Pamenepo anati kwa iye, Utiuzetu choipa ichi chatigwera chifukwa cha yani? Ntchito yako njotani? Ufuma kuti? Dziko lako nliti? Nanga mtundu wako?

9 Ndipo ananena nao, Ndine Muhebri, ndiopa Yehova Mulungu wa Kumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.

10 Pamenepo amunawo anaopa kwambiri, nati kwa iye, Ichi nchiyani wachichita? Pakuti amunawo anadziwa kuti anathawa pamaso pa Yehova, popeza adawauza.

11 Tsono anati kwa iye, Tichitenji nawe, kuti nyanja itichitire bata? Popeza namondwe anakulakulabe panyanja.

12 Ndipo anati nao, Mundinyamule ndi kundiponya m’nyanja, momwemo nyanja idzachitira inu bata; pakuti ndidziwa kuti namondwe wamkulu amene wakugwerani chifukwa cha ine.

13 Koma amunawo anapalasa kubwerera kumtunda, koma sanathe; pakuti namondwe wa panyanja anakulakula mokomana nao.

14 Pamenepo anafuulira kwa Yehova, nati, Tikupemphanitu, Yehova, tisatayike chifukwa cha moyo wa munthu uyu, musatisenzetse mwazi wosachimwa; pakuti, Inu Yehova, mwachita monga mudakomera Inu.

15 Momwemo ananyamula Yona, namponya m’nyanja; ndipo nyanja inaleka kukokoma kwake.

16 Ndipo amunawo anaopa Yehova ndi mantha aakulu, namphera Yehova nsembe, nawinda.

17 Koma Yehova anaikiratu chinsomba chachikulu chimeze Yona; ndipo Yona anali m’mimba mwa nsombayi masiku atatu usana ndi usiku.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JON/1-eec6119ff97f72a5cc6a099ea60f44b9.mp3?version_id=1068—

Categories
YONA

YONA 2

Pemphero la Yona ali m’mimba mwa chinsomba

1 Pamenepo Yona anapemphera kwa Yehova Mulungu wake ali m’mimba mwa nsombayo.

2 Ndipo anati,

Ndinaitana Yehova m’nsautso wanga,

ndipo anandiyankha ine;

ndinafuula ndili m’mimba ya manda,

ndipo munamva mau anga.

3 Pakuti munandiponya mwakuya m’kati mwa nyanja,

ndipo madzi anandizinga;

mafunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.

4 Ndipo ndinati, Ndatayika ndichoke pamaso panu;

koma ndidzapenyanso Kachisi wanu wopatulika.

5 Madzi anandizinga mpaka moyo wanga,

madzi akuya anandizungulira,

kayandeyande wa m’nyanja anandikulunga mutu.

6 Ndinatsikira kumatsinde a mapiri,

mipingiridzo ya dziko inanditsekereza kosatha;

koma munandikwezera moyo wanga

kuuchotsa kuchionongeko, Yehova Mulungu wanga.

7 Pokomoka moyo wanga m’kati mwanga ndinakumbukira Yehova;

ndi pemphero langa linafikira Inu mu Kachisi wanu wopatulika.

8 Iwo osamalira mabodza opanda pake

ataya chifundo chaochao.

9 Koma ine ndidzakupherani Inu nsembe ndi mau akuyamika,

ndidzakwaniritsa chowinda changa.

Chipulumutso ncha Yehova.

10 Pamenepo Yehova analankhula ndi nsombayo, ndipo inamsanzira Yona kumtunda.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JON/2-58e99d0de00220c8f33c33195a6f9d77.mp3?version_id=1068—

Categories
YONA

YONA 3

Yona ku Ninive. Kulapa kwa a ku Ninive

1 Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yona nthawi yachiwiri, ndi kuti,

2 Nyamuka, pita ku Ninive mzinda waukulu uja, nuulalikire uthenga umene ndikuuza.

3 Ndipo Yona ananyamuka, napita ku Ninive, monga mwa mau a Yehova. Koma Ninive ndiwo mzinda waukulu pamaso pa Yehova, wa ulendo wa masiku atatu.

4 Ndipo Yona anayamba kulowa mzindawo ulendo wa tsiku limodzi, nalalikira, nati, Atsala masiku makumi anai ndipo Ninive adzapasuka.

5 Ndipo anthu a Ninive anakhulupirira Mulungu, nalalikira chosala, navala chiguduli, kuyambira wamkulu kufikira wamng’ono wa iwowa.

6 Pakuti mau awa anafikira mfumu ya Ninive, ndipo inanyamuka kumpando wake wachifumu, nivula chofunda chake, nifunda chiguduli, nikhala m’maphulusa.

7 Ndipo analalikira, nanena mu Ninive mwa lamulo la mfumu ndi nduna zake, ndi kuti, Ngakhale munthu kapena nyama, ngakhale ng’ombe kapena nkhosa, zisalawe kanthu, zisadye, zisamwe madzi;

8 koma zifundidwe ndi chiguduli munthu ndi nyama, ndipo zifuulire kolimba kwa Mulungu; ndipo abwere yense kuleka njira yake yoipa, ndi chiwawa chili m’manja mwake.

9 Kaya, akatembenuka Mulungu, ndi kuleka kubwera ku mkwiyo wake waukali, kuti tisatayike.

10 Ndipo Mulungu anaona ntchito zao, kuti anabwera kuleka njira yao yoipa; ndipo Mulungu analeka choipa adanenachi kuti adzawachitira, osachichita.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JON/3-92e8214f7f0593aea9f5e7ae42a01d63.mp3?version_id=1068—

Categories
YONA

YONA 4

Kudandaula kwa Yona, kumdzudzula kwa Mulungu

1 Koma sikudakomere Yona konse, ndipo anapsa mtima.

2 Ndipo anapemphera kwa Yehova, nati, Ha, Yehova! Si ndiwo mau anga ndikali m’dziko langa? Chifukwa chake ndinafulumira kuthawira ku Tarisisi, pakuti ndinadziwa kuti Inu ndinu Mulungu wachisomo ndi wodzala chifundo, wolekerera ndi wokoma mtima mochuluka, ndi woleka choipacho.

3 Ndipo tsopano, Yehova, mundichotseretu moyo wanga, kundikomera ine kufa, osakhala ndi moyo ai.

4 Ndipo Yehova anati, Uyenera kupsa mtima kodi?

5 Pamenepo Yona anatuluka m’mzinda, nakhala pansi kum’mawa kwa mzinda, nadzimangira komweko thandala, nakhala pansi pake mumthunzi mpaka adzaona chochitikira mzinda.

6 Ndipo Yehova Mulungu anaikiratu msatsi, naumeretsera Yona, uchite mthunzi pamutu pake, kumlanditsa m’nsautso yake. Ndipo Yona anakondwera kwambiri chifukwa cha msatsiwo.

7 Koma Mulungu anauikira mphanzi pakucha m’mawa mwake, ndiyo inadya msatsi, nufota.

8 Ndipo kunali, potuluka dzuwa Mulungu anaika mphepo ya kum’mawa yotentha, ndipo dzuwa linatentha mutu wake wa Yona, nalefuka iye, nadzipempherera kuti afe; nati, Kundikomera ine kufa, kukhala ndi moyo ai.

9 Ndipo Mulungu anati kwa Yona, Uyenera kodi kupsa mtima chifukwa cha msatsiwo? Nati iye, Ee, kundiyenera ine kupsa mtima mpaka imfa.

10 Ndipo Yehova anati, Unachitira chifundo msatsiwo umene sunagwirepo ntchito, kapena kuumeretsa, umene unamera usiku, nutha usiku;

11 ndipo sindiyenera Ine kodi kuchitira chifundo Ninive mzinda waukulu uwu; m’mene muli anthu oposa zikwi zana limodzi mphambu zikwi makumi awiri osadziwa kusiyanitsa pakati padzanja lao lamanja ndi lamanzere, ndi zoweta zambiri zomwe?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JON/4-564daa16dc68aaf72129c732994fd76f.mp3?version_id=1068—