Categories
YOHANE

YOHANE 10

Za Mbusa Wabwino

1 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Iye wosalowa m’khola la nkhosa pakhomo, koma akwerera kwina, iyeyu ndiye wakuba ndi wolanda.

2 Koma iye wakulowera pakhomo, ndiye mbusa wa nkhosa.

3 Iyeyu, wapakhomo amtsegulira ndi nkhosa zimva mau ake; ndipo aitana nkhosa za iye yekha maina ao, nazitsogolera kunja.

4 Pamene adatulutsa zonse nkhosa zimtsata iye; chifukwa zidziwa mau ake.

5 Koma mlendo sizidzamtsata, koma zidzamthawa; chifukwa sizidziwa mau a alendo.

6 Fanizoili Yesu ananena kwa iwo; koma sanazindikire zimene Yesu analikulankhula nao.

7 Chifukwa chake Yesu ananenanso nao, Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Ine ndine khomo la nkhosa.

8 Onse amene anadza m’tsogolo mwa Ine ali akuba, ndi olanda: koma nkhosa sizinamve iwo.

9 Ine ndine khomo; ngati wina alowa ndi Ine, adzapulumutsidwa, nadzalowa, nadzatuluka, nadzapeza busa.

10 Siikudza mbala, koma kuti ikabe, ndi kupha, ndi kuononga. Ndadza Ine kuti akhale ndi moyo, ndi kukhala nao wochuluka.

11 Ine ndine Mbusa Wabwino; mbusa wabwino ataya moyo wake chifukwa cha nkhosa.

12 Wolipidwa amene sakhala mbusa, amene nkhosa sizili zake za yekha, aona mmbulu ulinkudza, nasiya nkhosazo, nathawa; ndipo mmbulu uzikwatula, nuzibalalitsa;

13 chifukwa ali wolipidwa, ndipo sasamala nkhosa.

14 Ine ndiye Mbusa Wabwino; ndipo ndizindikira zanga, ndi zanga zindizindikira Ine,

15 monga Atate andidziwa Ine, ndi Ine ndimdziwa Atate; ndipo nditaya moyo wanga chifukwa cha nkhosa.

16 Ndipo nkhosa zina ndili nazo, zimene sizili za khola ili; izinso ndiyenera kuzitenga, ndipo zidzamva mau anga; ndipo zidzakhala gulu limodzi, mbusa mmodzi.

17 Chifukwa cha ichi Atate andikonda Ine, chifukwa nditaya Ine moyo wanga, kuti ndikautengenso.

18 Palibe wina andichotsera uwu, koma ndiutaya Ine ndekha. Ndili nayo mphamvu yakuutaya, ndi mphamvu ndili nayo yakuutenganso; lamulo ili ndinalandira kwa Atate wanga.

19 Panakhalanso kutsutsana pakati pa Ayuda chifukwa cha mau awa.

20 Koma ambiri mwa iwo ananena, Ali ndi chiwanda, nachita misala; mukumva Iye bwanji?

21 Ena ananena, Mau awa sali a munthu wogwidwa chiwanda. Kodi chiwanda chikhoza kumtsegulira maso wosaona?

Yesu adziwulula ali Mwana wa Mulungu

22 Koma kunali phwando la kukonzetsanso muYerusalemu; nyengoyo ndi yachisanu.

23 Ndipo Yesu analikuyendayenda mu Kachisi m’khonde la Solomoni.

24 Pamenepo Ayuda anamzungulira Iye, nanena ndi Iye, Kufikira liti musinkhitsasinkhitsa moyo wathu? Ngati Inu ndinuKhristu, tiuzeni momveka.

25 Yesu anayankha iwo, Ndakuuzani, ndipo simukhulupirira. Ntchitozi ndidzichita Ine m’dzina la Atate wanga, zimenezi zindichitira umboni.

26 Koma inu simukhulupirira, chifukwa simuli a mwa nkhosa zanga.

27 Nkhosa zanga zimva mau anga, ndipo Ine ndizizindikira, ndipo zinditsata Ine.

28 Ndipo Ine ndizipatsa moyo wosatha; ndipo sizidzaonongeka kunthawi yonse, ndipo palibe munthu adzazikwatula m’dzanja langa.

29 Atate wanga, amene anandipatsa izo, ali wamkulu ndi onse; ndipo palibe wina ngathe kuzikwatula m’dzanja la Atate.

30 Ine ndi Atate ndife amodzi.

31 Ayuda anatolanso miyala kuti amponye Iye.

32 Yesu anayankha iwo, Ndakuonetsani inu ntchito zabwino zambiri za kwa Atate; chifukwa cha ntchito yiti ya izo mundiponya miyala?

33 Ayuda anamyankha Iye, Chifukwa cha ntchito yabwino sitikuponyani miyala, koma chifukwa cha mwano; ndi kuti Inu, muli munthu, mudziyesera nokha Mulungu.

34 Yesu anayankha iwo, Kodi sikulembedwa m’chilamulo chanu, Ndinati Ine, Muli milungu?

35 Ngati anawatcha milungu iwo amene mau a Mulungu anawadzera (ndipo cholemba sichingathe kuthyoka),

36 kodi inu munena za Iye, amene Atate anampatula namtuma kudziko lapansi, Uchita mwano; chifukwa ndinati, Ndili Mwana wa Mulungu?

37 Ngati sindichita ntchito za Atate wanga, musakhulupirira Ine.

38 Koma ngati ndichita, mungakhale simukhulupirira Ine, khulupirirani ntchitozo; kuti mukadziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndi Ine mwa Atate.

39 Anafunanso kumgwira Iye; ndipo anapulumuka m’dzanja lao.

40 Ndipo anachoka kunkanso tsidya lija la Yordani, kumalo kumene kunali Yohane analikubatiza poyamba paja; ndipo anakhala komweko.

41 Ndipo ambiri anadza kwa Iye; nanena kuti, Sanachita chizindikiro Yohane; koma zinthu zilizonse Yohane ananena za Iye zinali zoona.

42 Ndipo ambiri anakhulupirira Iye komweko.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/10-2d9027098beab02152a4207220b0b591.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE 11

Chiukitso cha Lazaro

1 Koma panali munthu wodwala, Lazaro wa ku Betaniya, wa m’mudzi wa Maria ndi mbale wake Marita.

2 Koma ndiye Maria uja anadzoza Ambuye ndi mafuta onunkhira bwino, napukuta mapazi ake ndi tsitsi lake, amene mlongo wake Lazaro anadwala.

3 Pamenepo alongo ake anatumiza kwa Iye, nanena, Ambuye, onani, amene mumkonda adwala.

4 Koma Yesu pamene anamva, anati, Kudwala kumene sikuli kwa imfa, koma chifukwa cha ulemerero wa Mulungu, kuti Mwana wa Mulungu alemekezedwe nako.

5 Koma Yesu anakonda Marita, ndi mbale wake, ndi Lazaro.

6 Chifukwa chake pamene anamva kuti anadwala, anakhala pamenepo pamalo pomwepo masiku awiri.

7 Ndipo pambuyo pake ananena kwaophunziraake, Tiyeni tipitenso ku Yudeya.

8 Ophunzira ananena ndi Iye,Rabi, Ayuda analikufuna kukuponyani miyala tsopano apa; ndipo munkanso komweko kodi?

9 Yesu anayankha, Kodi sikuli maora khumi ndi awiri usana? Ngati munthu ayenda usana sakhumudwa, chifukwa apenya kuunika kwa dziko lino lapansi.

10 Koma ngati munthu ayenda usiku, akhumudwa, chifukwa mulibe kuunika mwa iye.

11 Izi anati, ndipo zitatha izi ananena nao, Lazaro bwenzi lathu ali m’tulo; koma ndimuka kukamuukitsa iye tulo take.

12 Chifukwa chake ophunzira ake anati kwa Iye, Ambuye, ngati ali m’tulo adzachira.

13 Koma Yesu adanena za imfa yake; koma iwowa anayesa kuti ananena za mpumulo wa tulo.

14 Pamenepo Yesu anati kwa iwo momveka, Lazaro wamwalira.

15 Ndipo ndikondwera chifukwa cha inu kuti kunalibe Ine komweko, chakuti mukakhulupirire; koma tiyeni, tipite kwa iye.

16 Pamenepo Tomasi, wotchedwa Didimo, anati kwa ophunzira anzake, Tipite ifenso kuti tikafere naye pamodzi.

17 Ndipo pamene Yesu anadza, anapeza kuti pamenepo atakhala m’manda masiku anai.

18 Koma Betaniya anali pafupi paYerusalemu, nthawi yake yonga ya mastadiya khumi ndi asanu;

19 koma ambiri a mwa Ayuda adadza kwa Marita ndi Maria, kudzawatonthoza mtima pa mlongo wao.

20 Pamenepo Marita, pakumva kuti Yesu alinkudza, anamuka kukakomana ndi Iye; koma Maria anakhalabe m’nyumba.

21 Ndipo Marita anati kwa Yesu, Ambuye, mukadakhala kuno mlongo wanga sakadafa.

22 Koma ngakhale tsopano ndidziwa kuti zinthu zilizonse mukapempha Mulungu, adzakupatsani Mulungu.

23 Yesu ananena naye, Mlongo wako adzauka.

24 Marita ananena ndi Iye, Ndidziwa kuti adzauka m’kuuka tsiku lomaliza.

25 Yesu anati kwa iye, Ine ndine kuuka ndi moyo: wokhulupirira Ine, angakhale amwalira, adzakhala ndi moyo;

26 ndipo yense wakukhala ndi moyo, nakhulupirira Ine, sadzamwalira nthawi yonse. Kodi ukhulupirira ichi?

27 Ananena ndi Iye, Inde Ambuye; ndakhulupirira ine kuti Inu ndinuKhristu, Mwana wa Mulungu, wakudza m’dziko lapansi.

28 Ndipo m’mene anati ichi anachoka naitana Maria mbale wake m’tseri, ndi kuti, Wafika Mphunzitsi, akuitana iwe.

29 Koma iyeyo, pakumva, ananyamuka msanga, nadza kwa Iye.

30 (Koma Yesu sanafike kumudzi, koma anali pamalo pomwe Marita adakomana ndi Iye.)

31 Pamenepo Ayuda okhala naye m’nyumba, ndi kumtonthoza iye, pakuona Maria ananyamuka msanga, natuluka, namtsata iye, ndi kuyesa kuti amuka kumanda kukalira komweko.

32 Pomwepo Maria, pofika pamene panali Yesu, m’mene anamuona Iye, anagwa pa mapazi ake, nanena ndi Iye, Ambuye, mukadakhala kuno Inu, mlongo wanga sakadamwalira.

33 Pamenepo Yesu, pakumuona iye alikulira, ndi Ayuda akumperekeza iye alikulira, anadzuma mumzimu, navutika mwini,

34 nati, Mwamuika iye kuti? Ananena ndi Iye, Ambuye, tiyeni mukaone.

35 Yesu analira.

36 Chifukwa chake Ayuda ananena, Taonani, anamkondadi!

37 Koma ena mwa iwo anati, Kodi uyu wotsegulira maso wosaona uja, sakanatha kodi kuchita kuti asafe ameneyunso?

38 Pamenepo Yesu, ndi kudzumanso mwa Iye yekha anadza kumanda. Koma panali phanga, ndipo mwala unaikidwa pamenepo.

39 Yesu ananena, Chotsani mwala. Marita, mlongo wake wa womwalirayo, ananena ndi Iye, Ambuye, adayamba kununkha: pakuti wagona masiku anai.

40 Yesu ananena naye, Kodi sindinati kwa iwe, kuti, ngati ukhulupirira, udzaona ulemerero wa Mulungu?

41 Pomwepo anachotsa mwala. Koma Yesu anakweza maso ake kupenya kumwamba nati, Atate, ndiyamika Inu kuti munamva Ine.

42 Koma ndadziwa Ine kuti mumandimva Ine nthawi zonse; koma chifukwa cha khamu la anthu alikuimirira pozungulira ndinanena ichi, kuti akhulupirire kuti Inu munandituma Ine.

43 Ndipo m’mene adanena izi, anafuula ndi mau aakulu, Lazaro, tuluka.

44 Ndipo womwalirayo anatuluka womangidwa miyendo ndi manja ndi nsalu za kumanda; ndi nkhope yake inazingidwa ndi mlezo. Yesu ananena nao, Mmasuleni iye, ndipo mlekeni amuke.

45 Chifukwa chake ambiri a mwa Ayuda amene anadza kwa Maria, m’mene anaona chimene anachita, anakhulupirira Iye.

46 Koma ena a mwa iwo anamuka kwaAfarisi, nawauza zimene Yesu adazichita.

Afarisi apangana za kupha Yesu

47 Pamenepo ansembe aakulu ndi Afarisi anasonkhanitsa akulu, nanena, Titani ife? Chifukwa munthu uyu achita zizindikiro zambiri.

48 Ngati timleka Iye kotero, onse adzakhulupirira Iye; ndipo adzadza Aroma nadzachotsa malo athu ndi mtundu wathu.

49 Koma wina mmodzi wa mwa iwo, Kayafa, wokhala mkulu wa ansembe chaka chomwecho anati kwa iwo, Simudziwa kanthu konse inu,

50 kapena simuganiza kuti nkokoma kwa inu kuti munthu mmodzi afere anthu, ndi kuti mtundu wonse usaonongeke.

51 Koma ichi sananene kwa iye yekha; koma pokhala mkulu wa ansembe chaka chomwecho ananenera kuti Yesu adzafera mtunduwo;

52 ndipo si chifukwa cha mtunduwo wokha ai, koma kuti akasonkhanitse pamodzi ana a Mulungu akubalalikawo.

53 Chifukwa chake, kuyambira tsiku lomwelo anapangana kuti amuphe Iye.

54 Chifukwa chake Yesu sanayendeyendenso poonekera mwa Ayuda, koma anachokapo kunka kudziko loyandikira chipululu, kumudzi dzina lake Efuremu; nakhala komweko pamodzi ndi ophunzira ake.

55 KomaPaskawa Ayuda anali pafupi; ndipo ambiri anakwera kunka ku Yerusalemu kuchoka kuminda, asanafike Paska, kukadziyeretsa iwo okha.

56 Pamenepo analikumfuna Yesu, nanena wina ndi mnzake poimirira iwo mu Kachisi, Muyesa bwanji inu, sadzadza kuchikondwerero kodi?

57 Koma ansembe aakulu ndi Afarisi adalamula kuti, munthu wina akadziwa pokhala Iye, aulule, kuti akamgwire Iye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/11-e85eeb5710066782c0432fec7c6911ee.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE 12

Maria adzoza mapazi a Yesu

1 Pomwepo anatsala masiku asanu ndi limodzi asanafikePaska, Yesu anadza ku Betaniya kumene kunali Lazaro, amene Yesu adamuukitsa kwa akufa.

2 Ndipo anamkonzera Iye chakudya komweko; ndipo Marita anatumikira; koma Lazaro anali mmodzi wa iwo akuseama pachakudya pamodzi ndi Iye.

3 Pamenepo Maria m’mene adatenga muyeso umodzi wa mafuta onunkhira bwino anaridoweniweni a mtengo wake wapatali, anadzoza mapazi a Yesu, napukuta mapazi ake ndi tsitsi lake; ndipo nyumba inadzazidwa ndi mnunkho wake wa mafutawo.

4 Koma Yudasi Iskariote, mmodzi waophunziraake, amene adzampereka Iye, ananena,

5 Nanga mafuta onunkhira awa sanagulitsidwe chifukwa ninji ndi marupiya atheka mazana atatu, ndi kupatsidwa kwa osauka?

6 Koma ananena ichi si chifukwa analikusamalira osauka, koma chifukwa anali mbala, ndipo pokhala nalo thumba, amaba zoikidwamo.

7 Pamenepo Yesu anati, Mleke iye, pakuti anachisungira ichi tsiku la kuikidwa kwanga.

8 Pakuti osauka muli nao pamodzi ndi inu nthawi zonse; koma simuli ndi Ine nthawi zonse.

9 Pamenepo khamu lalikulu la Ayuda linadziwa kuti ali pomwepo; ndipo anadza, si chifukwa cha Yesu yekha, koma kuti adzaone Lazaro, amene adamuukitsa kwa akufa.

10 Koma ansembe aakulu anapangana kuti akaphe Lazaronso;

11 pakuti ambiri a Ayuda anachoka chifukwa cha iye, nakhulupirira Yesu.

Yesu alowa mu Yerusalemu

12 M’mawa mwake khamu lalikulu la anthu amene adadza kuchikondwerero, pakumva kuti Yesu alinkudza kuYerusalemu,

13 anatenga makwata a kanjedza, natuluka kukakomana ndi Iye, nafuula, Hosana; wolemekezeka Iye wakudza m’dzina la Ambuye, ndiye mfumu ya Israele.

14 Koma Yesu, m’mene adapeza kabulu anakhala pamenepo; monga mulembedwa:

15 Usaope, mwana wamkazi waZiyoni; taona mfumu yako idza wokhala pa mwana wa bulu.

16 Izi sanazidziwe ophunzira ake poyamba; koma pamene Yesu analemekezedwa, pamenepo anakumbukira kuti izi zinalembedwa za Iye, ndi kuti adamchitira Iye izi.

17 Pamenepo khamulo limene linali pamodzi ndi Iye, m’mene anaitana Lazaro kutuluka kumanda, namuukitsa kwa akufa, anachita umboni.

18 Chifukwa cha ichinso khamulo linadza kudzakomana ndi Iye, chifukwa anamva kuti Iye adachita chizindikiro ichi.

19 Chifukwa chakeAfarisiananena wina ndi mnzake, Muona kuti simupindula kanthu konse; onani dziko litsata pambuyo pake pa Iye.

Agriki afuna kuona Yesu; Iye ayankhapo

20 Koma panali Agriki ena mwa iwo akukwera kunka kukalambira pachikondwerero.

21 Ndipo iwo anadza kwa Filipo wa ku Betsaida wa mu Galileya, namfunsa iye, ndi kuti, Mbuye, tifuna kuona Yesu.

22 Filipo anadza nanena kwa Andrea; nadza Andrea ndi Filipo, nanena ndi Yesu.

23 Koma Yesu anayankha iwo, nati, Yafika nthawi, kutiMwana wa Munthualemekezedwe.

24 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Ngati mbeu ya tirigu siigwa m’nthaka, nifa, ikhala pa yokha iyo; koma ngati ifa, ibala chipatso chambiri.

25 Iye wokonda moyo wake adzautaya; ndipo wodana ndi moyo wake m’dziko lino lapansi adzausungira kumoyo wosatha.

26 Ngati wina anditumikira Ine, anditsate; ndipo kumene kuli Ine, komwekonso kudzakhala mtumiki wanga. Ngati wina anditumikira Ine, Atate adzamchitira ulemu iyeyu.

27 Moyo wanga wavutika tsopano; ndipo ndidzanena chiyani? Atate, ndipulumutseni Ine kunthawi iyi. Koma chifukwa cha ichi ndinadzera nthawi iyi.

28 Atate, lemekezani dzina lanu. Pomwepo adadza mau ochokera Kumwamba, Ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.

29 Chifukwa chake khamu la anthu akuimirirako, ndi kuwamva ananena kuti kwagunda. Ena ananena,Mngelowalankhula ndi Iye.

30 Yesu anayankha nati, Mau awa sanafike chifukwa cha Ine, koma cha inu.

31 Tsopano pali kuweruza kwa dziko ili lapansi; mkulu wa dziko ili lapansi adzatayidwa kunja tsopano.

32 Ndipo Ine, m’mene ndikakwezedwa kudziko, ndidzakoka anthu onse kwa Ine ndekha.

33 Koma ananena ichi ndi kuzindikiritsa imfa yanji akuti adzafa nayo.

34 Pamenepo khamulo linayankha Iye, Tidamva ife m’chilamulo kutiKhristuakhala kunthawi yonse; ndipo Inu munena bwanji, kuti Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa? Mwana wa Munthu amene ndani?

35 Pamenepo Yesu anati kwa iwo, Katsala kanthawi kakang’ono ndipo kuunika kuli mwa inu. Yendani pokhala muli nako kuunika, kuti mdima sungakupezeni; ndipo woyenda mumdima sadziwa kumene amukako.

36 Pokhala muli nako kuunika, khulupirirani kuunikako, kuti mukakhale ana a kuunikako. Izi Yesu analankhula, nachoka nawabisalira.

37 Koma angakhale adachita zizindikiro zambiri zotere pamaso pao iwo sanakhulupirire Iye;

38 kuti mau a Yesayamneneriakakwaniridwe, amene anati,

Ambuye, wakhulupirira ndani kulalikira kwathu?

Ndipo mkono wa Ambuye wavumbulutsidwa kwa yani?

39 Chifukwa cha ichi sanathe kukhulupirira, pakuti Yesaya anatinso,

40 Wadetsa maso ao, naumitsa mtima wao;

kuti angaone ndi maso, angazindikire ndi mtima,

nangatembenuke,

ndipo ndingawachiritse.

41 Izi anati Yesaya, chifukwa anaona ulemerero wake; nalankhula za Iye.

42 Kungakhale kotero, ambiri a mwa akulu anakhulupirira Iye; koma chifukwa cha Afarisi sanavomereze, kuti angaletsedwe m’sunagoge,

43 pakuti anakonda ulemerero wa anthu koposa ulemerero wa Mulungu.

44 Koma Yesu anafuula nati, Iye wokhulupirira Ine, sakhulupirira Ine, koma Iye wondituma Ine.

45 Ndipo wondiona Ine aona amene anandituma Ine.

46 Ndadza Ine kuunika kudziko lapansi, kuti yense wokhulupirira Ine asakhale mumdima.

47 Ndipo ngati wina akumva mau anga, ndi kusawasunga, Ine sindimweruza; pakuti sindinadze kudzaweruza dziko lapansi, koma kuti ndipulumutse dziko lapansi.

48 Iye amene akaniza Ine, ndi kusalandira mau anga, ali naye womweruza iye, mau amene ndalankhula, iwowa adzamweruza tsiku lomaliza.

49 Pakuti sindinalankhule mwa Ine ndekha; koma Atate wondituma Ine, yemweyu anandipatsa Ine lamulo, limene ndikanene, ndi limene ndikalankhule.

50 Ndipo ndidziwa kuti lamulo lake lili moyo wosatha; chifukwa chake zimene ndilankhula, monga momwe Atate wanena ndi Ine, momwemo ndilankhula.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/12-1f37420411c52cd5e734bf7b45793ec3.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE 13

Yesu asambitsa mapazi a anyamata ake

1 Koma pasanafike chikondwerero laPaska, Yesu, podziwa kuti nthawi yake idadza yakuchoka kutuluka m’dziko lino lapansi, kunka kwa Atate, m’mene anakonda ake a Iye yekha a m’dziko lapansi, anawakonda kufikira chimaliziro.

2 Ndipo pokhala pamgonero, mdierekezi adatha kuika mu mtima wake wa Yudasi mwana wa Simoni Iskariote, kuti akampereke Iye,

3 Yesu, podziwa kuti Atate adampatsa Iye zonse m’manja mwake, ndi kuti anachokera kwa Mulungu, namuka kwa Mulungu,

4 ananyamuka pamgonero, navula malaya ake; ndipo m’mene adatenga chopukutira, anadzimanga m’chuuno.

5 Pomwepo anathira madzi m’beseni, nayamba kusambitsa mapazi aophunziraake, ndi kuwapukuta ndi chopukutira, chimene anadzimanga nacho.

6 Anadza pomwepo kwa Simoni Petro. Iyeyu ananena ndi Iye, Ambuye, kodi Inu mundisambitsa ine mapazi?

7 Yesu anayankha nati kwa iye, Chimene ndichita Ine suchidziwa tsopano; koma udzadziwa m’tsogolo mwake.

8 Petro ananena ndi Iye, Simudzasambitsa mapazi anga kunthawi yonse. Yesu anamyankha iye, Ngati sindikusambitsa iwe ulibe cholandira pamodzi ndi Ine.

9 Simoni Petro ananena ndi Iye, Ambuye, si mapazi anga okha, komanso manja ndi mutu.

10 Yesu ananena naye, Amene anatha kusamba alibe kusowa koma kusamba mapazi, koma ayera monse: ndipo inu ndinu oyera, koma si nonse ai.

11 Pakuti anadziwa amene adzampereka Iye; chifukwa cha ichi anati, Simuli oyera nonse.

12 Pamenepo, atatha Iye kusambitsa mapazi ao, ndi kutenga malaya ake, anaseamanso, nati kwa iwo, Nanga chimene ndakuchitirani inu, muchizindikira kodi?

13 Inu munditcha Ine Mphunzitsi, ndi Ambuye: ndipo munena bwino; pakuti ndine amene.

14 Chifukwa chake, ngati Ine Ambuye ndi Mphunzitsi, ndasambitsa mapazi anu, inunso muyenera kusambitsana mapazi wina ndi mnzake.

15 Pakuti ndakupatsani inu chitsanzo, kuti, monga Ine ndakuchitirani inu, inunso muchite.

16 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Kapolo sali wamkulu ndi mbuye wake; kapena mtumwi sali wamkulu ndi womtuma iye.

17 Ngati mudziwa izi, odala inu ngati muzichita.

18 Sindinena za inu nonse; ndidziwa amene ndawasankha: koma kuti cholemba chikwaniridwe, Iye wakudya mkate wanga anatsalimira pa Ine chidendene chake.

19 Kuyambira tsopano ndinena kwa inu, chisadachitike, kuti pamene chitachitika, mukakhulupirire kuti ndine amene.

20 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Iye wolandira aliyense amene ndimtuma, andilandira Ine; koma wolandira Ine alandira wondituma Ine.

Yesu aneneratu kuti Yudasi adzampereka

21 Yesu m’mene adanena izi, anavutika mumzimu, nachita umboni, nati, Indetu, indetu, ndinena ndi inu, kuti mmodzi wa inu adzandipereka Ine.

22 Ophunzira analikupenyana wina kwa mnzake, ndi kusinkhasinkha kuti ananena za yani.

23 Koma mmodzi wa ophunzira ake, amene Yesu anamkonda, analikutsamira pa chifuwa cha Yesu.

24 Pamenepo Simoni Petro anamkodola nanena naye, Utiuze ndiye yani amene anena za iye.

25 Iyeyu potsamira pomwepo, pa chifukwa cha Yesu, anena ndi Iye, Ambuye, ndiye yani?

26 Ndipo Yesu anayankha, Ndi iyeyu, amene Ine ndidzamsunsira nthongo ndi kumpatsa. Pamenepo, m’mene anasunsa nthongo anaitenga naipatsa Yudasi mwana wa Simoni Iskariote.

27 Ndipo pambuyo pake pa nthongoyo,Satanaanalowa mwa iyeyu. Pamenepo Yesu ananena naye, Chimene uchita, chita msanga.

28 Koma palibe mmodzi wa iwo akuseamako anadziwa chimene anafuna, poti atere naye.

29 Pakuti popeza Yudasi anali nalo thumba, ena analikuyesa kuti Yesu ananena kwa iye, Gula zimene zitisowa pachikondwerero; kapena, kuti apatse kanthu kwa aumphawi.

30 Pamenepo iyeyo m’mene adalandira nthongo, anatuluka pomwepo. Koma kunali usiku.

31 Tsono m’mene adatuluka, Yesu ananena, Tsopano walemekezekaMwana wa Munthu, ndipo Mulungu walemekezedwa mwa Iye;

32 ndipo Mulungu adzamlemekeza Iye mwa Iye yekha, adzamlemekeza Iye tsopano apa.

33 Tiana, katsala kanthawi ndikhala ndi inu. Mudzandifunafuna Ine; ndipo monga ndinanena kwa Ayuda, kuti kumene ndinkako Ine, inu simungathe kudza, momwemo ndinena kwa inu tsopano.

34 Ndikupatsani inu lamulo latsopano, kuti mukondane wina ndi mnzake; monga ndakonda inu, kuti inunso mukondane wina ndi mnzake.

35 Mwa ichi adzazindikira onse kuti muli ophunzira anga, ngati muli nacho chikondano wina ndi mnzake.

Yesu aneneratu kuti Petro adzamkana

36 Simoni Petro anena ndi Iye, Ambuye, mumuka kuti? Yesu anayankha, Kumene ndimukako sungathe kunditsata Ine tsopano; koma, udzanditsata bwino lomwe.

37 Petro ananena ndi Iye, Ambuye, sindingathe kukutsatani Inu tsopano chifukwa ninji? Ndidzataya moyo wanga chifukwa cha Inu.

38 Yesu anayankha, Moyo wako kodi udzautaya chifukwa cha Ine? Indetu, indetu, ndinena kwa iwe, Asanalire tambala udzandikana Ine katatu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/13-1a9da6e94b820b49a9bac217ef84589d.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE 14

Yesu aneneratu za kubweranso kwake

1 Mtima wanu usavutike; mukhulupirira Mulungu, khulupirirani Inenso.

2 M’nyumba ya Atate wanga alimo malo okhalamo ambiri. Ngati sikudali kutero, ndikadakuuzani inu; pakuti ndipita kukukonzerani inu malo.

3 Ndipo ngati ndipita kukakonzera inu malo, ndidzabweranso, ndipo ndidzalandira inu kwa Ine ndekha; kuti kumene kuli Ineko, mukakhale inunso.

4 Ndipo kumene ndinkako Ine, mudziwa njira yake.

5 Tomasi ananena ndi Iye, Ambuye, sitidziwa kumene munkako; tidziwa njira bwanji?

6 Yesu ananena naye, Ine ndine njira, ndi choonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.

Yesu ndi Atate ndiwo amodzi

7 Mukadazindikira Ine mukadadziwa Atate wanganso; kuyambira tsopano mumzindikira Iye, ndipo mwamuona Iye.

8 Filipo ananena ndi Iye, Ambuye, tionetsereni ife Atate, ndipo chitikwanira.

9 Yesu ananena naye, Kodi ndili ndi inu nthawi yaikulu yotere, ndipo sunandizindikire, Filipo? Iye amene wandiona Ine waona Atate; unena iwe bwanji, Mutionetsere Atate?

10 Sukhulupirira kodi kuti ndili Ine mwa Atate, ndi Atate ali mwa Ine? Mau amene ndinena Ine kwa inu sindilankhula kwa Ine ndekha; koma Atate wokhala mwa Ine achita ntchito zake.

11 Khulupirirani Ine, kuti Ine ndili mwa Atate ndi Atate ali mwa Ine; koma ngati si chomwecho, khulupirirani Ine chifukwa cha ntchito zomwe.

12 Indetu, indetu, ndinena kwa inu, Wokhulupirira Ine, ntchito zimene ndichita Ine adzazichitanso iyeyu; ndipo adzachita zoposa izi; chifukwa ndipita Ine kwa Atate.

13 Ndipo chimene chilichonse mukafunse m’dzina langa, ndidzachichita, kuti Atate akalemekezedwe mwa Mwana.

14 Ngati mudzapempha kanthu m’dzina langa, ndidzachita.

15 Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.

Lonjezo la Mzimu Woyera

16 Ndipo Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani inu Nkhoswe ina, kuti akhale ndi inu kunthawi yonse,

17 ndiye Mzimu wa choonadi; amene dziko lapansi silingathe kumlandira, pakuti silimuona Iye, kapena kumzindikira Iye. Inu mumzindikira Iye; chifukwa akhala ndi inu nadzakhala mwa inu.

18 Sindidzakusiyani inu mukhale ana amasiye; ndidza kwa inu.

19 Katsala kanthawi, ndipo dziko lapansi silindionanso Ine; koma inu mundiona; popeza Ine ndili ndi moyo inunso mudzakhala ndi moyo.

20 Tsiku lomwelo mudzazindikira kuti ndili Ine mwa Atate wanga, ndi inu mwa Ine, ndi Ine mwa inu.

21 Iye wakukhala nao malamulo anga, ndi kuwasunga, iyeyu ndiye wondikonda Ine; koma wondikonda Ine adzakondedwa ndi Atate wanga, ndipo Ine ndidzamkonda, ndipo ndidzadzionetsa ndekha kwa iye.

22 Yudasi, si Iskariote, ananena ndi Iye, Ambuye, chachitika chiyani kuti muziti mudzionetsa nokha kwa ife, koma si kwa dziko lapansi?

23 Yesu anayankha nati kwa iye, Ngati wina akonda Ine, adzasunga mau anga; ndipo Atate wanga adzamkonda, ndipo tidzadza kwa iye, ndipo tidzayesa kwa iye mokhalamo.

24 Wosandikonda Ine sasunga mau anga; ndipo mau amene mumva sali mau anga, koma a Atate wondituma Ine.

25 Izi ndalankhula nanu, pakukhala ndi inu.

26 Koma Nkhosweyo, Mzimu Woyera, amene Atate adzamtuma m’dzina langa, Iyeyo adzaphunzitsa inu zonse, nadzakumbutsa inu zinthu zonse zimene ndinanena kwa inu.

Mphatso ya mtendere

27 Mtendere ndikusiyirani inu, mtendere wanga ndikupatsani; Ine sindikupatsani inu monga dziko lapansi lipatsa. Mtima wanu usavutike, kapena usachite mantha.

28 Mwamva kuti Ine ndinanena kwa inu, Ndimuka, ndipo ndidza kwa inu. Mukadandikonda Ine, mukadakondwera kuti ndipita kwa Atate; pakuti Atate ali wamkulu ndi Ine.

29 Ndipo tsopano ndakuuzani chisanachitike, kuti pamene chitachitika mukakhulupirire.

30 Sindidzalankhulanso zambiri ndi inu, pakuti mkulu wa dziko lapansi adza; ndipo alibe kanthu mwa Ine;

31 koma kuti dziko lapansi lizindikire kuti ndikonda Atate, ndi kuti ndichita monga momwe Atate wandilamula. Nyamukani, tizimuka kuchokera kuno.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/14-4094d0cbc7cf5196f979c0b55986f2ae.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE 15

Mpesa ndi nthambi zake

1 Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate wanga ndiye wam’munda.

2 Nthambi iliyonse ya mwa Ine yosabala chipatso, aichotsa; ndi iliyonse yakubala chipatso, aisadza, kuti ikabale chipatso chochuluka.

3 Mwakhala okonzeka tsopano inu chifukwa cha mau amene ndalankhula ndi inu.

4 Khalani mwa Ine, ndi Ine mwa inu. Monga nthambi siingathe kubala chipatso pa yokha, ngati siikhala mwampesa; motere mulibe inunso ngati simukhala mwa Ine.

5 Ine ndine mpesa, inu ndinu nthambi zake: wakukhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye, ameneyo abala chipatso chambiri; pakuti kopanda Ine simungathe kuchita kanthu.

6 Ngati wina sakhala mwa Ine, watayika kunja monga nthambi, nafota; ndipo azisonkhanitsa nazitaya kumoto, nazitentha.

7 Ngati mukhala mwa Ine, ndi mau anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene muchifuna ndipo chidzachitika kwa inu.

8 Mwa ichi alemekezedwa Atate wanga, kuti mubale chipatso chambiri; ndipo mudzakhalaophunziraanga.

9 Monga momwe Atate wandikonda Ine, Inenso ndakonda inu; khalani m’chikondi changa.

10 Ngati musunga malamulo anga mudzakhala m’chikondi changa; monga Ine ndasunga malamulo a Atate wanga, ndipo ndikhala m’chikondi chake.

11 Izi ndalankhula ndi inu, kuti chimwemwe changa chikhale mwa inu, ndi kuti chimwemwe chanu chidzale.

12 Lamulo langa ndi ili, kuti mukondane wina ndi mnzake, monga ndakonda inu.

13 Palibe munthu ali nacho chikondi choposa ichi, chakuti munthu ataya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.

14 Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulani inu.

Chiyanjano chatsopano

15 Sinditchanso inu akapolo; chifukwa kapolo sadziwa chimene mbuye wake achita; koma ndatcha inu abwenzi; chifukwa zonse zimene ndazimva kwa Atate wanga ndakudziwitsani.

16 Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani inu, ndipo ndinakuikani, kuti mukamuke inu ndi kubala chipatso, ndi kuti chipatso chanu chikhale; kuti chimene chilichonse mukapempha Atate m’dzina langa akakupatseni inu.

17 Zinthu izi ndilamula inu, kuti mukondane wina ndi mnzake.

Wokhulupirira pokhala padziko lapansi

18 Ngati dziko lapansi lida inu, mudziwa kuti lidada Ine lisanayambe kuda inu.

19 Mukadakhala a dziko lapansi, dziko lapansi likadakonda zake za lokha; koma popeza simuli a dziko lapansi, koma Ine ndinakusankhani inu mwa dziko lapansi, chifukwa cha ichi likudani inu.

20 Kumbukirani mau amene Ine ndinanena kwa inu, Kapolo sali wamkulu ndi mbuye wake. Ngati anandilondalonda Ine, adzakulondalondani inunso; ngati anasunga mau anga, adzasunga anunso.

21 Koma izi zonse adzakuchitirani chifukwa cha dzina langa, chifukwa sadziwa wondituma Ine.

22 Sindikadadza ndi kulankhula nao sakadakhala nalo tchimo; koma tsopano alibe chowiringula pa machimo ao.

23 Iye wondida Ine, adanso Atate wanga.

24 Sindikadachita mwa iwo ntchito zosachita wina, sakadakhala nalo tchimo; koma tsopano anaona, nada Ine ndi Atate wanganso.

25 Koma chitero, kuti mau olembedwa m’chilamulo chao akwaniridwe, kuti, Anandida Ine kopanda chifukwa.

Mzimu Woyera ndi ophunzira omwe adzachita umboni

26 Koma pamene wafika Nkhoswe, amene Ine ndidzamtuma kwa inu kuchokera kwa Atate, ndiye Mzimu wa choonadi, amene atuluka kwa Atate, Iyeyu adzandichitira Ine umboni.

27 Ndipo inunso muchita umboni, pakuti muli ndi Ine kuyambira chiyambi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/15-f08f4f9e4665b53fdfb7ae3efac92b5f.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE 16

Awachenjeza za kuzunzidwa

1 Izi ndalankhula ndi inu kuti mungakhumudwitsidwe.

2 Adzakutulutsani m’masunagoge, koma ikudza nthawi imene yense wakupha inu adzayesa kuti atumikira Mulungu.

3 Ndipo izi adzachita, chifukwa sanadziwe Atate, kapena Ine.

4 Koma zinthu izi ndalankhula ndi inu kuti ikadza nthawi yao, mukakumbukire kuti ndinakuuzani. Koma izi sindinanene kwa inu kuyambira pachiyambi, chifukwa ndinali pamodzi ndi inu.

5 Koma tsopano ndimuka kwa Iye wondituma Ine; ndipo palibe wina mwa inu andifunsa Ine, Munka kuti?

6 Koma chifukwa ndalankhula izi ndi inu chisoni chadzala mumtima mwanu.

Chomwe Mzimu Woyera adzachitira anthu

7 Koma ndinena Ine choonadi ndi inu; kuyenera kwa inu kuti ndichoke Ine; pakuti ngati sindichoka, Nkhosweyo sadzadza kwa inu; koma ngati ndipita ndidzamtuma Iye kwa inu.

8 Ndipo atadza Iyeyo, adzatsutsa dziko lapansi za machimo, ndi za chilungamo, ndi za chiweruziro;

9 za machimo, chifukwa sakhulupirira Ine;

10 za chilungamo, chifukwa ndinka kwa Atate, ndipo simundionanso;

11 za chiweruzo, chifukwa mkulu wa dziko ili lapansi waweruzidwa.

12 Ndili nazo zambirinso zakunena kwa inu, koma simungathe kuzisenza tsopano lino.

13 Koma atadza Iyeyo, Mzimu wa choonadi, adzatsogolera inu m’choonadi chonse; pakuti sadzalankhula za Iye mwini; koma zinthu zilizonse adzazimva, adzazilankhula; ndipo zinthu zilinkudza adzakulalikirani.

14 Iyeyo adzalemekeza Ine; chifukwa adzatenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu.

15 Zinthu zilizonse Atate ali nazo ndi zanga; chifukwa chake ndinati, kuti atenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu.

Yesu anena za imfa, kuuka, ndikubwera kwake

16 Katsala kanthawi, ndipo simundionanso Ine, ndipo kanthawinso, ndipo mudzandiona Ine.

17 Mwaophunziraake tsono anati wina ndi mnzake, Ichi nchiyani chimene anena ndi ife, Kanthawi ndipo simundione; ndiponso kanthawi, ndipo mudzandiona; ndipo, chifukwa ndimuka kwa Atate?

18 Chifukwa chake ananena. Ichi nchiyani chimene anena, Kanthawi? Sitidziwa chimene alankhula.

19 Yesu anazindikira kuti analikufuna kumfunsa Iye, ndipo anati kwa iwo, Kodi mulikufunsana wina ndi mnzake za ichi, kuti ndinati, Kanthawi ndipo simundiona Ine, ndiponso kanthawi nimudzandiona Ine?

20 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, kuti mudzalira ndi kubuma maliro inu, koma dziko lapansi lidzakondwera; mudzachita chisoni inu, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe.

21 Mkazi pamene akuti abale ali nacho chisoni, chifukwa yafika nthawi yake; koma pamene wabala mwana, sakumbukiranso kusaukako, chifukwa cha chimwemwe kuti wabadwa munthu kudziko lapansi.

22 Ndipo inu tsono muli nacho chisoni tsopano lino, koma ndidzakuonaninso, ndipo mtima wanu udzakondwera, ndipo palibe wina adzachotsa kwa inu chimwemwe chanu.

23 Ndipo tsiku limenelo simudzandifunsa kanthu. Indetu, indetu, ndinena kwa inu, Ngati mudzapempha Atate kanthu, adzakupatsani inu m’dzina langa.

24 Kufikira tsopano simunapemphe kanthu m’dzina langa; pemphani, ndipo mudzalandira, kuti chimwemwe chanu chikwaniridwe.

25 Zinthu izi ndalankhula ndi inu m’mafanizo; ikudza nthawi imene sindidzalankhula ndi inu m’mafanizo, koma ndidzakulalikirani inu m’mafanizo, koma ndidzakulalikirani inu momveka za Atate.

26 Tsiku limenelo mudzapempha m’dzina langa; ndipo sindinena kwa inu kuti Ine ndidzafunsira inu kwa Atate;

27 pakuti Atate yekha akonda inu, chifukwa inu mwandikonda Ine, ndi kukhulupirira kuti Ine ndinatuluka kwa Atate.

28 Ndinatuluka mwa Atate, ndipo ndadza kudziko lapansi: ndilisiyanso dziko lapansi, ndipo ndipita kwa Atate.

29 Ophunzira ake ananena, Onani, tsopano mulankhula zomveka, ndipo mulibe kunena chiphiphiritso.

30 Tsopano tidziwa kuti mudziwa zonse, ndipo mulibe kusowa kuti wina akafunse Inu; mwa ichi tikhulupirira kuti munatuluka kwa Mulungu.

31 Yesu anayankha iwo, Kodi mukhulupirira tsopano?

32 Onani ikudza nthawi, ndipo yafika, imene mudzabalalitsidwa, yense ku zake za yekha, ndipo mudzandisiya Ine pa ndekha. Ndipo sindikhala pa ndekha, chifukwa Atate ali pamodzi ndi Ine,

33 Zinthu izi ndalankhula ndi inu, kuti mwa Ine mukakhale nao mtendere. M’dziko lapansi mudzakhala nacho chivuto, koma limbikani mtima; ndalingonjetsa dziko lapansi Ine.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/16-0d694d9b5dfb2f886a65aff789de101c.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE 17

Yesu apempherera ophunzira ake

1 Zinthu izi analankhula Yesu; ndipo m’mene anakweza maso ake Kumwamba, anati, Atate, yafika nthawi; lemekezani Mwana wanu, kuti Mwana wanu akulemekezeni Inu;

2 monga mwampatsa Iye ulamuliro pa thupi lililonse, kuti onse amene mwampatsa Iye, awapatse iwo moyo wosatha.

3 Koma moyo wosatha ndi uwu, kuti akadziwe Inu Mulungu woona yekha, ndi YesuKhristuamene munamtuma.

4 Ine ndalemekeza Inu padziko lapansi, m’mene ndinatsiriza ntchito imene munandipatsa ndichite.

5 Ndipo tsopano, Atate Inu, lemekezani Ine ndi Inu nokha ndi ulemerero umene ndinali nao ndi Inu lisanakhale dziko lapansi.

6 Ndalionetsera dzina lanu kwa anthu amene mwandipatsa Ine m’dziko lapansi; anali anu, ndipo mwandipatsa Ine iwo; ndipo adasunga mau anu.

7 Azindikira tsopano kuti zinthu zilizonse zimene mwandipatsa Ine zichokera kwa Inu;

8 chifukwa mau amene munandipatsa Ine ndinapatsa iwo; ndipo analandira, nazindikira koona kuti ndinatuluka kwa Inu, ndipo anakhulupirira kuti Inu munandituma Ine.

9 Ine ndiwapempherera iwo; sindipempherera dziko lapansi, koma iwo amene mwandipatsa Ine,

10 chifukwa ali anu: ndipo zanga zonse zili zanu, ndi zanu zili zanga; ndipo ndilemekezedwa mwa iwo.

11 Sindikhalanso m’dziko lapansi, koma iwo ali m’dziko lapansi, ndipo Ine ndidza kwa Inu. Atate Woyera, sungani awa m’dzina lanu amene mwandipatsa Ine, kuti akhale mmodzi, monga Ife.

12 Pamene ndinakhala nao, Ine ndinalikuwasunga iwo m’dzina lanu amene mwandipatsa Ine; ndipo ndinawasunga, ndipo sanatayike mmodzi yense wa iwo, koma mwana wa chitayiko, kuti lembo likwaniridwe.

13 Koma tsopano ndidza kwa Inu; ndipo izi ndilankhula m’dziko lapansi, kuti akhale nacho chimwemwe changa chokwaniridwa mwa iwo okha.

14 Ine ndawapatsa iwo mau anu; ndipo dziko lapansi, linadana nao, chifukwa sakhala a dziko lapansi, monga Ine sindikhala wa dziko lapansi.

15 Sindipempha kuti muwachotse iwo m’dziko lapansi, koma kuti muwasunge iwo kuletsa woipayo.

16 Siali a dziko lapansi monga Ine sindili wa dziko lapansi.

17 Patulani iwo m’choonadi; mau anu ndi choonadi.

18 Monga momwe munandituma Ine kudziko lapansi, Inenso ndinatuma iwo kudziko lapansi.

19 Ndipo chifukwa cha iwo Ine ndidzipatula ndekha kuti iwonso akhale opatulidwa m’choonadi.

20 Koma sindipempherera iwo okha, komanso iwo akukhulupirira Ine chifukwa cha mau ao;

21 kuti onse akakhale amodzi, monga Inu Atate mwa Ine, ndi Ine mwa Inu, kuti iwonso akakhale mwa Ife: kuti dziko lapansi likakhulupirire kuti Inu munandituma Ine.

22 Ndipo ulemerero umene mwandipatsa Ine ndapatsa iwo; kuti akhale amodzi, monga Ife tili mmodzi;

23 Ine mwa iwo, ndi Inu mwa Ine, kuti akhale angwiro mwa mmodzi; kuti dziko lapansi lizindikire kuti Inu munandituma Ine, nimunawakonda iwo, monga momwe munakonda Ine.

24 Atate, amene mwandipatsa Ine, ndifuna kuti, kumene ndili Ine, iwonso akhale pamodzi ndi Ine; kuti ayang’anire ulemerero wanga, umene mwandipatsa Ine; pakuti munandikonda Ine lisanakhazikike dziko lapansi.

25 Atate wolungama, dziko lapansi silinadziwe Inu, koma Ine ndinadziwa Inu; ndipo iwo anazindikira kuti munandituma Ine;

26 ndipo ndinazindikiritsa iwo dzina lanu, ndipo ndidzalizindikiritsa; kuti chikondi chimene munandikonda nacho chikhale mwa iwo, ndi Ine mwa iwo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/17-d24043e80e76ebc6264a063e5a768ae6.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE 18

Yesu mu Getsemani

1 M’mene Yesu adanena izi, anatuluka ndiophunziraake, kunka tsidya lija la mtsinje wa Kidroni, kumene kunali munda, umene analowamo Iye ndi ophunzira ake.

Aperekedwa namangidwa

2 Koma Yudasinso amene akampereka Iye, anadziwa malowa; chifukwa Yesu akankako kawirikawiri ndi ophunzira ake.

3 Pamenepo Yudasi, m’mene adatenga gulu la asilikali ndi anyamata, kwa ansembe aakulu ndiAfarisi, anadza komweko ndi nyali ndi miuni ndi zida.

4 Pamenepo Yesu, podziwa zonse zilinkudza pa Iye, anatuluka, nati kwa iwo, Mufuna yani?

5 Anayankha Iye, Yesu Mnazarayo. Yesu ananena nao, Ndine. Koma Yudasi yemwe, wompereka Iye, anaima nao pamodzi.

6 Ndipo m’mene anati kwa iwo, Ndine, anabwerera m’mbuyo, nagwa pansi.

7 Pamenepo anawafunsanso, Mufuna yani? Koma iwo anati, Yesu Mnazarayo.

8 Yesu anayankha, Nati, Ndine; chifukwa chake ngati mufuna Ine, lekani awa amuke;

9 kuti akwaniridwe mau amene ati, Mwa iwo amene mwandipatsa Ine, sindinataye mmodzi.

10 Pamenepo Simoni Petro pokhala nalo lupanga, analisolola nakantha kapolo wa mkulu wa ansembe, namsenga khutu lake lamanja. Koma dzina lake la kapoloyo ndiye Malkusi.

11 Pamenepo Yesu anati kwa Petro, Longa lupanga m’chimake chake; chikho chimene Atate wandipatsa Ine sindimwere ichi kodi?

Yesu kwa mkulu wa ansembe. Petro amkana

12 Ndipo khamulo ndi kapitao wamkulu, ndi anyamata a Ayuda anagwira Yesu nammanga Iye,

13 nayamba kupita naye kwa Anasi; pakuti anali mpongozi wa Kayafa, amene anali mkulu wa ansembe chaka chomwecho.

14 Koma Kayafa anali uja wakulangiza Ayuda, kuti kuyenera munthu mmodzi afere anthu.

15 Koma Simoni Petro ndi wophunzira wina anatsata Yesu. Koma wophunzira ameneyo anali wodziwika kwa mkulu wa ansembe, nalowa pamodzi ndi Yesu, m’bwalo la mkulu wa ansembe;

16 koma Petro anaima kukhomo kunja. Chifukwa chake wophunzira winayo amene anadziwika kwa mkulu wa ansembe, anatuluka nalankhula ndi wapakhomo, nalowetsa Petro.

17 Pamenepo mdzakazi wapakhomoyo ananena kwa Petro, Kodi suli iwenso wa ophunzira a munthu uyu? Iyeyu ananena, Sindine.

18 Koma akapolo anyamata analikuimirirako, atasonkha moto wamakala; pakuti kunali kuzizira; ndipo analikuotha moto; koma Petronso anali nao alikuimirira ndi kuotha moto.

19 Ndipo mkulu wa ansembe anafunsa Yesu za ophunzira ake, ndi chiphunzitso chake.

20 Yesu anayankha iye, Ine ndalankhula zomveka kwa dziko lapansi; ndinaphunzitsa Ine nthawi zonse m’sunagogendi mu Kachisi, kumene amasonkhana Ayuda onse; ndipo mobisika sindinalankhule kanthu.

21 Undifunsiranji Ine? Funsa iwo amene adamva chimene ndinalankhula nao; taona, amenewo adziwa chimene ndinanena Ine.

22 Koma m’mene Iye adanena izi, mmodzi wa anyamata akuimirirako anapanda Yesu khofu, ndi kuti, Kodi uyankha mkulu wa ansembe chomwecho?

23 Yesu anayankha iye, Ngati ndalankhula choipa, chita umboni wa choipacho, koma ngati bwino, undipandiranji?

24 Koma Anasi adamtumiza Iye womangidwa kwa Kayafa mkulu wa ansembe.

25 Koma Simoni Petro analikuimirira ndi kuotha moto. Pomwepo anati kwa iye, Suli iwenso wa ophunzira ake kodi? Iyeyu anakana, nati, Sindine.

26 Mmodzi wa akapolo a mkulu wa ansembe ndiye mbale wake uja amene Petro anamdula khutu, ananena, Ine sindinakuone iwe kodi m’munda pamodzi ndi Iye?

27 Pamenepo Petro anakananso; ndipo pomwepo analira tambala.

Yesu kwa Pilato

28 Pamenepo anamtenga Yesu kuchokera kwa Kayafa kupita ku Pretorio; koma munali mamawa; ndipo iwo sanalowe ku Pretorio, kuti angadetsedwe, koma kuti akadyePaska.

29 Chifukwa chake Pilato anatulukira kunja kwa iwo, nati, Chifukwa chanji mwadza nacho cha munthu uyu?

30 Anayankha nati kwa iye, Akadakhala wosachita zoipa uyu sitikadampereka Iye kwa inu.

31 Ndipo Pilato anati kwa iwo, Mumtenge Iye inu, ndi kumweruza Iye monga mwa chilamulo chanu. Ayuda anati kwa iye, Tilibe ulamuliro wakupha munthu aliyense;

32 kuti mau a Yesu akwaniridwe, amene ananena akuzindikiritsa imfa imene akuti adzafa nayo.

33 Chifukwa chake Pilato analowanso mu Pretorio, naitana Yesu, nati kwa Iye, Iwe ndiwe mfumu ya Ayuda kodi?

34 Yesu anayankha, Kodi munena ichi mwa inu nokha, kapena ena anakuuzani za Ine?

35 Pilato anayankha, Ndili ine Myuda kodi? Mtundu wako ndi ansembe aakulu anakupereka kwa ine; wachita chiyani?

36 Yesu anayankha, Ufumu wanga suli wa dziko lino lapansi; ufumu wanga ukadakhala wa dziko lino lapansi, anyamata anga akadalimbika nkhondo, kuti ndisaperekedwe kwa Ayuda; koma tsopano ufumu wanga suli wochokera konkuno.

37 Pamenepo Pilato anati kwa Iye, Nanga kodi ndiwe Mfumu? Yesu anayankha, Munena kuti ndine Mfumu. Ndinabadwira ichi Ine, ndipo ndinadzera ichi kudza kudziko lapansi, kuti ndikachite umboni ndi choonadi. Yense wakukhala mwa choonadi amva mau anga.

38 Pilato ananena kwa Iye, Choonadi nchiyani? Ndipo pamene adanena ichi, anatulukiranso kwa Ayudawo, nanena nao, Ine sindipeza konse chifukwa mwa Iye.

39 Koma muli nao makhalidwe, akuti ndimamasulira inu mmodzi pa Paska; kodi mufuna tsono kuti ndimasulire inu mfumu ya Ayuda?

40 Pomwepo anafuulanso, nanena, Si uyu, koma Barabasi. Koma Barabasi anali wachifwamba.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/18-dd4e80ee86e50858bec18eff645a647c.mp3?version_id=1068—

Categories
YOHANE

YOHANE 19

1 Pamenepo tsono Pilato anatenga Yesu, namkwapula.

2 Ndipo asilikali, m’mene analuka korona waminga anamveka pamutu pake, namfunda Iye malaya achibakuwa;

3 nadza kwa Iye, nanena, Tikuoneni, mfumu ya Ayuda! Nampanda khofu.

4 Ndipo Pilato anatulukanso kunja, nanena nao, Taonani, ndidza naye kwa inu kunja kuti mudziwe kuti sindipeza mwa Iye chifukwa chilichonse.

5 Pamenepo Yesu anatuluka kunja, atavala korona waminga, ndi malaya achibakuwa. Ndipo ananena nao, Taonani munthuyu!

6 Ndipo pamene ansembe aakulu ndi anyamata anamuona Iye, anafuula nanena, Mpachikeni, mpachikeni. Pilato ananenana nao, Mtengeni Iye inu nimumpachike; pakuti ine sindipeza chifukwa mwa Iye.

7 Ayuda anamyankha iye, Tili nacho chilamulo ife, ndipo monga mwa chilamulocho ayenera kufa, chifukwa anadziyesera Mwana wa Mulungu.

8 Ndipo pamene Pilato anamva mau awa, anaopa koposa.

9 Ndipo analowanso ku Pretorio, nanena kwa Yesu, Muchoka kuti? Koma Yesu sanamyankhe kanthu.

10 Chifukwa chake Pilato ananena kwa Iye, Simulankhula ndi ine kodi? Simudziwa kodi kuti ulamuliro ndili nao wakukumasulani, ndipo ndili nao ulamuliro wakukupachikani?

11 Yesu anamyankha iye, Simukadakhala nao ulamuliro uliwonse pa Ine, ngati sukadapatsidwa kwa inu kuchokera Kumwamba; chifukwa cha ichi iye wondipereka Ine kwa inu ali nalo tchimo loposa.

12 Pa ichi Pilato anafuna kumasula Iye; koma Ayuda anafuula, ndi kunena, Ngati mumasula ameneyo, simuli bwenzi laKaisara; yense wodziyesera yekha mfumu atsutsana naye Kaisara.

13 Pamenepo Pilato, m’mene adamva mau awa, anatuluka ndi Yesu, nakhala pansi pa mpando woweruzira kumalo dzina lake, Bwalo lamiyala, koma mu Chihebri, Gabata.

14 Koma linali tsiku lokonzaPaska; panali monga ora lachisanu ndi chimodzi. Ndipo ananena kwa Ayuda, Taonani, mfumu yanu!

15 Pamenepo anafuula iwowa, Chotsani, Chotsani, mpachikeni Iye! Pilato ananena nao, Ndipachike mfumu yanu kodi? Ansembe aakulu anayankha, Tilibe mfumu koma Kaisara.

16 Ndipo pamenepo anampereka Iye kwa iwo kuti ampachike.

Ampachika Yesu pamtanda

Pamenepo anatenga Yesu;

17 ndipo anasenza mtanda yekha, natuluka kunka kumalo otchedwa Malo a Bade, amene atchedwa mu Chihebri, Gologota:

18 kumene anampachika Iye; ndipo pamodzi ndi Iye awiri ena, chakuno ndi chauko, koma Yesu pakati.

19 Koma Pilato analemba lembo, naliika pamtanda. Koma panalembedwa, YESU MNAZARAYO, MFUMU YA AYUDA.

20 Ndipo lembo ilo analiwerenga ambiri a Ayuda; chifukwa malo amene Yesu anapachikidwapo anali pafupi pa mzindawo; ndipo linalembedwa mu Chihebri, ndi mu Chilatini, ndi mu Chigriki.

21 Pamenepo ansembe aakulu a Ayuda, ananena kwa Pilato, Musalembe, Mfumu ya Ayuda; koma kuti Iyeyu anati, Ndili mfumu ya Ayuda.

22 Pilato anayankha, Chimene ndalemba, ndalemba.

23 Pamenepo asilikali, m’mene adapachika Yesu, anatenga zovala zake, anadula panai, natenga wina china, wina china, ndiponso malaya; koma malaya anaombedwa monsemo kuyambira pamwamba pake, analibe msoko.

24 Chifukwa chake anati wina kwa mnzake, Tisang’ambe awa, koma tichite maere, awa akhale a yani; kuti lembo likwaniridwe limene linena, Anagawana zovala zanga mwa iwo okha, ndi pa malaya anga anachitira maere. Ndipo asilikali anachita izi.

25 Koma pamtanda wa Yesu anaimirira amake, ndi mbale wa amake, Maria, mkazi wa Kleopa, ndi Maria wa Magadala.

26 Pamenepo Yesu pakuona amake, ndi wophunziraamene anamkonda, alikuimirirako, ananena kwa amake, Mkazi, taonani, mwana wanu!

27 Pamene ananena kwa wophunzirayo, Taona, amai wako. Ndipo kuyambira ora lomweli wophunzirayo ananka naye kwao.

Yesu afa pamtanda

28 Chitapita ichi Yesu, podziwa kuti zonse zidatha pomwepo kuti lembo likwaniridwe, ananena, Ndimva ludzu.

29 Kunaikidwako chotengera chodzala ndi vinyo wosasayo pa phesi lahisope, nachifikitsa kukamwa kwake.

30 Pamene Yesu tsono adalandira vinyo wosasayo anati, Kwatha; ndipo anawerama mutu, napereka mzimu.

Sathyola miyendo ya Yesu

31 Pomwepo Ayuda, popeza panali tsiku lokonzera, kuti mitembo ingatsale pamtanda tsiku la Sabata, pakuti tsiku lomwelo la Sabata linali lalikulu, anapempha Pilato kuti miyendo yao ithyoledwe, ndipo achotsedwe.

32 Chifukwa chake anadza asilikali nathyola miyendo ya woyambayo, ndi ya winayo wopachikidwa pamodzi ndi Iye;

33 koma pofika kwa Yesu, m’mene anamuona Iye, kuti wafa kale, sanathyole miyendo yake;

34 koma mmodzi wa asilikali anamgwaza ndi nthungo m’nthiti yake, ndipo panatuluka pomwepo mwazi ndi madzi.

35 Ndipo iye amene anaona, wachita umboni, ndi umboni wake uli woona; ndipo iyeyu adziwa kuti anena zoona, kuti inunso mukakhulupirire.

36 Pakuti izi zinachitika, kuti lembo likwaniridwe, Fupa la Iye silidzathyoledwa.

37 Ndipo linenanso lembo lina, Adzayang’ana pa Iye amene anampyoza.

Kuikidwa kwa Yesu

38 Chitatha ichi Yosefe wa ku Arimatea, ndiye wophunzira wa Yesu, koma mobisika, chifukwa cha kuopa Ayuda, anapempha Pilato kuti akachotse mtembo wa Yesu. Ndipo Pilato analola. Chifukwa chake anadza, nachotsa mtembo wake.

39 Koma anadzanso Nikodemo, amene anadza kwa Iye usiku poyamba paja, alikutenga chisakanizo chamurendi aloe, monga miyeso zana.

40 Pamenepo anatenga mtembo wa Yesu, nauzenenga ndi nsalu zabafuta pamodzi ndi zonunkhira, monga mwa maikidwe a maliro a Ayuda.

41 Koma kunali munda kumalo kumene anapachikidwako, ndi m’mundamo munali manda atsopano m’mene sanaikidwemo munthu aliyense nthawi zonse.

42 Pomwepo ndipo anaika Yesu, chifukwa cha tsiku lokonzera la Ayuda, pakuti mandawo anali pafupi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/19-67d413f75a0a4afcb034097e8ceb475c.mp3?version_id=1068—