Categories
YOBU

YOBU 20

Zofari afotokozera masautso amene Mulungu atumizira oipa

1 Pamenepo anayankha Zofari Mnaama, nati,

2 M’mwemo zolingirira zanga zindiyankha,

chifukwa chake ndifulumidwa m’kati mwanga.

3 Ndamva kudzudzula kwakundichititsa manyazi,

ndi mzimu wa nzeru yanga undiyankha.

4 Kodi suchidziwa ichi chiyambire kale lomwe,

kuyambira anaika munthu padziko lapansi,

5 kuti kufuula kokondwera kwa woipa sikukhalira kutha,

ndi chimwemwe cha wonyoza Mulungu chikhala kamphindi?

6 Chinkana ukulu wake ukwera kunka kuthambo,

nugunda pamitambo mutu wake;

7 koma adzatayika kosatha ngati zonyansa zake;

iwo amene adamuona adzati, Ali kuti iye?

8 Adzauluka ngati loto, osapezekanso;

nadzaingidwa ngati masomphenya a usiku.

9 Diso lidamuonalo silidzamuonanso;

ndi malo ake sadzampenyanso.

10 Ana ake adzapempha aumphawi awakomere mtima;

ndi manja ake adzabweza chuma chake.

11 Mafupa ake adzala nao unyamata wake,

koma udzagona naye pansi m’fumbi.

12 Chinkana choipa chizuna m’kamwa mwake,

chinkana achibisa pansi pa lilime lake;

13 chinkana achisunga, osachileka,

nachikhalitsa m’kamwa mwake;

14 koma chakudya chake chidzasandulika m’matumbo mwake,

chidzakhala ndulu ya mphiri m’kati mwake.

15 Anachimeza chuma koma adzachisanzanso;

Mulungu adzachitulutsa m’mimba mwake.

16 Adzayamwa ndulu ya mphiri;

pakamwa pa njoka padzamupha.

17 Sadzapenyerera timitsinje,

toyenda nao uchi ndi mafuta.

18 Chimene adagwiriracho ntchito, adzachibweza, osachimeza;

sadzakondwera monga mwa zolemera zake adaziona.

19 Pakuti anapsinja, nasiya aumphawi;

analanda nyumba mwachiwawa, imene sanaimange.

20 Popeza sanadziwe kupumula m’kati mwake,

sadzalanditsa kanthu ka zofunika zake.

21 Sikunatsalira kanthu kosadya iye,

chifukwa chake zokoma zake sizidzakhalitsa.

22 Pomkwanira kudzala kwake adzakhala m’kusauka;

dzanja la yense wovutika lidzamgwera.

23 Poti adzaze mimba yake,

Mulungu adzamponyera mkwiyo wake waukali,

nadzamvumbitsira uwu pakudya iye.

24 Adzathawa chida chachitsulo,

ndi muvi wa uta wamkuwa udzampyoza.

25 Auzula, nutuluka m’thupi mwake;

inde nsonga yonyezimira ituluka m’ndulu mwake;

zamgwera zoopsa.

26 Zamdima zonse zimsungikira zikhale chuma chake,

moto wosaukoleza munthu udzampsereza;

udzatha wotsalira m’hema mwake.

27 M’mwamba mudzavumbulutsa mphulupulu yake,

ndi dziko lapansi lidzamuukira.

28 Phindu la m’nyumba mwake lidzachoka,

akatundu ake adzamthawa tsiku la mkwiyo wake.

29 Ili ndi gawo la munthu woipa, lochokera kwa Mulungu,

ndi cholowa amuikiratu Mulungu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/20-749c414de1a2b9df99f584fdf38a538e.mp3?version_id=1068—

Categories
YOBU

YOBU 21

Yobu ayankha kuti oipa ambiri amalemerera. Zooneka m’maso sizitiuza za mtima wa Mulungu

1 Pamenepo Yobu anayankha, nati,

2 Mvetsetsani mau anga;

ndi ichi chikhale chitonthozo chanu.

3 Mundilole, ndinene nanenso;

ndipo nditanena ine, sekani.

4 Kodi ine, kudandaula kwanga, ndidandaulira munthu?

Ndipo ndilekerenji kupsa mtima?

5 Ndiyang’anireni, nimusumwe,

gwirani pakamwa panu.

6 Ndikangokumbukira ndivutika mtima,

ndi thupi langa lichita nyaunyau.

7 Oipa akhaliranji ndi moyo,

nakalamba, nalemera kwakukulu?

8 Mbeu zao zikhazikika pamodzi nao pankhope pao,

ndi ana ao pamaso pao.

9 Nyumba zao sizitekeseka ndi mantha,

ngakhale ndodo ya Mulungu siiwakhalira.

10 Ng’ombe yao yamphongo imakwera, yosakanika;

ng’ombe yao yaikazi imaswa, yosapoloza.

11 Atulutsa makanda ao ngati gulu,

ndi ana ao amavinavina.

12 Aimbira lingaka ndi zeze,

nakondwera pomveka chitoliro.

13 Atsekereza masiku ao ndi zokoma,

natsikira m’kamphindi kumanda.

14 Koma adati kwa Mulungu, Tichokereni;

pakuti sitifuna kudziwa njira zanu.

15 Wamphamvuyonse ndiye yani kuti timtumikire?

Ndipo tidzapindulanji pakumpemphera Iye?

16 Taonani, zokoma zao sizili m’dzanja lao;

(koma uphungu wa oipa unditalikira.)

17 Ngati nyali za oipa zizimidwa kawirikawiri?

Ngati tsoka lao liwagwera?

Ngati Mulungu awagawira zowawa mu mkwiyo wake?

18 Ngati akunga ziputu zomka ndi mphepo,

ngati mungu wouluzika ndi nkuntho?

19 Mukuti, Mulungu asungira ana ake a munthu choipa chake,

ambwezere munthuyo kuti achidziwe.

20 Aone yekha chionongeko chake m’maso mwake,

namwe mkwiyo wa Wamphamvuyonse.

21 Pakuti chomsamalitsa nyumba yake nchiyani, atapita iye,

chiwerengo cha miyezi yake chitadulidwa pakati?

22 Ngati pali munthu wakumphunzitsa Mulungu nzeru?

Popeza Iye aweruza mlandu iwo okwezeka.

23 Wina akufa, wabiriwiri,

ali chikhalire ndi chipumulire.

24 Mbale zake zidzala ndi mkaka;

ndi wongo wa m’mafupa ake uli momwe.

25 Koma mnzake akufa ali nao mtima wakuwawa,

osalawa chokoma konse.

26 Iwo agona chimodzimodzi kufumbi,

ndi mphutsi ziwakuta.

27 Taonani, ndidziwa maganizo anu,

ndi chiwembu mundilingirira moipa.

28 Pakuti munena, Ili kuti nyumba ya kalonga?

Ndi hema wokhalamo woipa ali kuti?

29 Simunawafunsa kodi opita m’njira?

Ndipo simusamalira zotsimikiza zao?

30 Zakuti munthu woipa asungika tsiku la tsoka?

Natulutsidwa tsiku la mkwiyo?

31 Adzamfotokozera ndani njira yake pamaso pake?

Nadzamlipitsa ndani pa ichi anachichita?

32 Potsiriza pake adzapita naye kumanda,

nadzadikira pamanda pake.

33 Zibuma za kuchigwa zidzamkomera.

Adzakoka anthu onse amtsate,

monga anamtsogolera osawerengeka.

34 Potero munditonthozeranji nazo zopanda pake,

popeza m’mayankho mwanu mutsala mabodza okha?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/21-111450dd7ce8b948d17130bcf97f6156.mp3?version_id=1068—

Categories
YOBU

YOBU 22

Elifazi amtchulira Yobu zoipa zambiri, namuuza alape, Mulungu nadzamchitira chifundo

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,

2 Kodi munthu apindulira Mulungu?

Koma wanzeru angodzipindulira yekha.

3 Kodi Wamphamvuyonse akondwera nako

kuti iwe ndiwe wolungama?

Kapena kodi apindula nako kuti ukwaniritsa njira zako?

4 Kodi akudzudzula, nadza nawe kumlandu,

chifukwa cha kumuopa kwako?

5 Zoipa zako sizichuluka kodi?

Ndi mphulupulu zako sizikhala zosawerengeka kodi?

6 Pakuti wamtenga chikole kwa mbale wako wopanda chifukwa,

ndi kuvula ausiwa zovala zao.

7 Sunampatsa wolema madzi amwe,

ndi wanjala unammana chakudya.

8 Koma munthu mwini mphamvu, dziko ndi lake;

ndi munthu wovomerezeka, anakhala momwemo.

9 Unabweza akazi amasiye osawaninkha kanthu,

ndi manja a ana amasiye anathyoledwa.

10 Chifukwa chake misampha ikuzinga.

Ndi mantha akuvuta modzidzimutsa,

11 kapena mdima kuti ungaone,

ndi madzi aunyinji akumiza.

12 Kodi Mulungu sakhala m’mwamba m’tali?

Ndipo penyani kutalika kwake kwa nyenyezi, zili m’talitali.

13 Ndipo ukuti, Adziwa chiyani Mulungu?

Aweruza kodi mwa mdima wa bii?

14 Mitambo ndiyo chomphimba, kuti angaone;

ndipo amayenda pa thambo lakumwamba.

15 Udzasunga kodi njira yakale,

anaiponda anthu amphulupulu?

16 Amene anakwatulidwa isanafike nyengo yao,

chigumula chinakokolola kuzika kwao;

17 amene anati kwa Mulungu, Tichokereni;

ndipo, Angatichitire chiyani Wamphamvuyonse?

18 Angakhale Iye adadzaza nyumba zao ndi zabwino;

koma uphungu wa oipa unditalikira.

19 Olungama achiona nakondwera;

ndi osalakwa awaseka pwepwete,

20 ndi kuti, Zoonadi, otiukirawo alikhidwa,

ndi zowatsalira, moto unazipsereza.

21 Uzolowerane ndi Iye, nukhale ndi mtendere;

ukatero zokoma zidzakudzera.

22 Landira tsono chilamulo pakamwa pake,

nuwasunge maneno ake mumtima mwako.

23 Ukabweranso kwa Wamphamvuyonse, udzamanga bwino;

ukachotsera chosalungama kutali kwa mahema ako.

24 Ndipo utaye chuma chako kufumbi,

ndi golide wa ku Ofiri ku miyala ya kumitsinje.

25 Ndipo Wamphamvuyonse adzakhala chuma chako,

ndi ndalama zako zofunika.

26 Pakuti pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuyonse,

ndi kuweramutsa nkhope yako kwa Mulungu.

27 Udzampemphera ndipo adzakumvera;

nudzatsiriza zowinda zako.

28 Ukatsimikiza mtima kakuti, kadzakhazikikira iwe;

ndi kuunika kudzawala panjira zako.

29 Anthu akakugwetsa pansi, udzati, Adzandikweza;

ndipo adzapulumutsa wodzichepetsayo.

30 Adzamasula ngakhale wopalamula,

inde adzamasuka mwa kuyera kwa manja ako.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/22-0c8eaf0ad4df2bd7f5ecabd45970a9c9.mp3?version_id=1068—

Categories
YOBU

YOBU 23

Yobu abwereza kukana kuti sanachimwe. Mulungu wosadziwika achita chifuniro chake. Kwambiri ochimwa oyenera kulangidwa akhala bwino m’moyo uno

1 Koma Yobu anayankha, nati,

2 Lero lomwe kudandaula kwanga kumawawa;

kulanga kwanga kuposa kubuula kwanga m’kulemera kwake.

3 Ha! Ndikadadziwa kumene ndikampeza Mulungu,

kuti ndifike kumpando wake!

4 Ndikadalongosola mlandu wanga pamaso pake,

ndikadadzaza m’kamwa mwanga ndi matsutsano.

5 Ndikadadziwa mau akadandiyankha ine,

ndikadazindikira chimene akadanena nane.

6 Akadatsutsana nane kodi mwa mphamvu yake yaikulu?

Iai, koma akadanditcherera khutu.

7 Apo woongoka mtima akadatsutsana naye;

ndipo ndikadapulumuka chipulumukire kwa Woweruza wanga.

8 Taonani, ndikanka m’tsogolo, kulibe Iye;

kapena m’mbuyo sindimzindikira;

9 akachita Iye kulamanzere, sindimpenyerera;

akabisala kulamanja, sindimuona.

10 Koma adziwa njira ndilowayi;

atandiyesa ndidzatuluka ngati golide.

11 Phazi langa lagwiratu moponda Iye,

ndasunga njira yake, wosapatukamo.

12 Sindinabwerera kusiya malamulo a pa milomo yake;

ndasungitsa mau a pakamwa pake koposa lamulo langalanga.

13 Koma Iye ndiye wa mtima umodzi, adzambweza ndani?

Ndi ichi chimene moyo wake uchifuna achichita.

14 Pakuti adzachita chondiikidwiratu;

ndipo zambiri zotere zili ndi Iye.

15 Chifukwa chake ndiopsedwa pankhope pake;

ndikalingirira, ndichita mantha ndi Iye.

16 Pakuti Mulungu walefula mtima wanga,

ndi Wamphamvuyonse wandiopsa.

17 Popeza sindinalikhidwa usanafike mdimawo,

ndipo sanandiphimbire nkhope yanga ndi mdima wa bii.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/23-19fdf6c1cbf04aed83d4155c5d4aa7c3.mp3?version_id=1068—

Categories
YOBU

YOBU 24

1 Wamphamvuyonse alekeranji kuikiratu nyengo?

Ndi iwo omdziwa alekeranji kudziwa masiku ake?

2 Alipo akusendeza malire;

alanda gulu la zoweta, nazidyetsa.

3 Akankhizira kwao bulu wa amasiye,

atenga ng’ombe ya mfedwa ikhale chikole.

4 Apatukitsa aumphawi m’njira;

osauka a padziko abisala pamodzi.

5 Taonani, ngati mbidzi za m’chipululu

atulukira kuntchito zao, nalawirira nkufuna chakudya;

chipululu chiwaonetsera chakudya cha ana ao.

6 Atema dzinthu zao m’munda;

natola khunkha m’munda wampesa wa woipa.

7 Agona amaliseche usiku wonse opanda chovala,

alibe chofunda pachisanu.

8 Avumbwa ndi mvula kumapiri,

nafukata thanthwe posowa pousapo.

9 Akwatula wamasiye kubere,

natenga chikole chovala cha osauka;

10 momwemo ayenda amaliseche opanda chovala,

nasenza mtolo wa dzinthu ali ndi njala.

11 M’kati mwa malinga a iwo aja ayenga mafuta;

aponda mphesa moponderamo, namva ludzu.

12 M’mzinda waukulu anthu abuula alinkufa;

ndi moyo wa iwo olasidwa ufuula;

koma Mulungu sasamalira choipacho.

13 Iwo ndiwo amene apikisana nako kuunika,

sadziwa njira zake, Sasunga mayendedwe ake.

14 Kukacha auka wambanda, napha wosauka ndi waumphawi;

ndi usiku asanduka mbala.

15 Ndipo diso la wachigololo liyembekezera chisisira,

ndi kuti, Palibe diso lidzandiona;

navala chophimba pankhope pake.

16 Kuli mdima aboola nyumba,

usana adzitsekera,

osadziwa kuunika.

17 Pakuti iwo onse auyesa m’mawa mthunzi wa imfa;

pakuti adziwa zoopsa za mthunzi wa imfa.

18 Atengedwa ngati choyandama pamadzi;

gawo lao litembereredwa padziko;

sadzalunjikanso njira ya minda yampesa.

19 Chilala ndi dzuwa zitha madzi a chipale chofewa,

momwemo manda achita nao ochimwa.

20 M’mimba mudzamuiwala;

mphutsi zidzamudya mokondwera.

Sadzamkumbukiranso;

ndipo chosalungama chidzathyoledwa ngati mtengo.

21 Alusira chumba wosabala,

osamchitira wamasiye chokoma.

22 Mulungu awakhalitsa amphamvu mwa mphamvu yake;

iwo aukanso m’mene anayesa kuti sadzakhala ndi moyo.

23 Awalola akhale osatekeseka, ndipo alimbikapo;

koma maso ake ali panjira zao.

24 Akwezeka; m’kamphindi kuli zii;

inde atsitsidwa, achotsedwa monga ena onse,

adulidwa ngati tirigu ngala zake.

25 Ndipo ngati si kutero, anditsutsa ndani kuti ndili wabodza,

ndi kuyesa mau anga opanda pake?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/24-0ebef2528ceab784f33c50d5003ebd31.mp3?version_id=1068—

Categories
YOBU

YOBU 25

Bilidadi akuti munthu sayenera kudziyesa wolungama pamaso pa Mulungu

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha, nati,

2 Kulamulira ndi kuopsa kuli ndi Iye;

achita mtendere pa zam’mwamba zake.

3 Ngati awerengedwa makamu ake?

Ndipo ndaniyo, kuunika kwake sikumtulukira?

4 Potero munthu akhala bwanji wolungama kwa Mulungu?

Kapena wobadwa ndi mkazi akhala woyera bwanji?

5 Taonani, ngakhale mwezi ulibe kuwala;

ndi nyenyezi siziyera pamaso pake;

6 kopambana kotani nanga munthu, ndiye mphutsi!

Ndi wobadwa ndi munthu, ndiye nyongolotsi!

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/25-f6bb25ba6efb11ddaf8650d6fe9dea13.mp3?version_id=1068—

Categories
YOBU

YOBU 26

Yobu atsutsa Bilidadi kuti sanamthandize; yekha nalemekeza ukulu wa Mulungu

1 Koma Yobu anayankha, nati,

2 Wamthandiza bwanji wopanda mphamvu.

Kulipulumutsa dzanja losalimba!

3 Wampangira bwanji wopanda nzeruyu!

Ndi kudziwitsa nzeru zenizeni mochuluka!

4 Wafotokozera yani mau?

Ndi mzimu wa yani unatuluka mwa iwe?

5 Adafawo anjenjemera

pansi pamadzi ndi zokhalamo.

6 Kumanda kuli padagu pamaso pake,

ndi kuchionongeko kusowa chophimbako.

7 Ayala kumpoto popanda kanthu,

nalenjeka dziko pachabe.

8 Amanga madzi m’mitambo yake yochindikira;

ndi mtambo sung’ambika pansi pake.

9 Atchingira pa mpando wake wachifumu,

nayalapo mtambo wake.

10 Analembera madziwo malire,

mpaka polekeza kuunika ndi mdima.

11 Mizati ya thambo injenjemera,

ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.

12 Mwa mphamvu yake agwetsa nyanja bata;

ndipo mwa luntha lake akantha kudzikuza kwake.

13 Mwa mzimu wake anyezimiritsa thambo;

dzanja lake linapyoza njoka yothawayo.

14 Taonani, awa ndi malekezero a njira zake;

ndi chimene tikumva za Iye ndi chinong’onezo chaching’ono;

koma kugunda kwa mphamvu yake akuzindikiritsa ndani?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/26-db742895a2bb224dcb871d6449c6d54e.mp3?version_id=1068—

Categories
YOBU

YOBU 27

Yobu adzikaniza nanenetsa kuti ochimwa ambiri akhala osalangidwa. Ena ali ndi nzeru ndi chuma, koma opanda nzeru yeniyeni

1 Ndipo Yobu anaonjezanso mwambi wake, nati,

2 Pali Mulungu, amene anandichotsera zoyenera ine,

ndi Wamphamvuyonse, amene anawawitsa moyo wanga,

3 pakuti moyo wanga wonse ukali mwa ine,

ndi mpweya wa Mulungu m’mphuno mwanga;

4 milomo yanga siilankhula chosalungama,

ndi lilime langa silitchula zachinyengo.

5 Sindivomereza konse kuti muli olungama;

mpaka kufa ine sinditaya ungwiro wanga.

6 Ndiumirira chilungamo changa, osachileka;

chikhalire moyo ine, mtima wanga sunditonza.

7 Mdani wanga akhale ngati woipa,

ndi iye amene andiukira ngati wosalungama.

8 Pakuti chiyembekezo cha wonyoza Mulungu nchiyani pomlikhatu Mulungu,

pomchotsera moyo wake?

9 Kodi Mulungu adzamvera kufuula kwake, ikamdzera nsautso?

10 Kodi adzadzikondweretsa naye Wamphamvuyonse,

ndi kuitana kwa Mulungu nthawi zonse?

11 Ndidzakulangizani za dzanja la Mulungu;

chokhala ndi Wamphamvuyonse sindidzachibisa.

12 Taonani, inu nonse munachiona;

ndipo mugwidwa nazo zopanda pake chifukwa ninji?

13 Ili ndi gawo la munthu woipa kwa Mulungu,

ndi cholowa cha akupsinja anzao achilandira kwa Wamphamvuyonse.

14 Akachuluka ana ake, ndiko kuchulukira lupanga,

ndi ana ake sadzakhuta chakudya.

15 Akumtsalira iye adzaikidwa muimfa,

ndi akazi ake amasiye sadzalira maliro.

16 Chinkana akundika ndalama ngati fumbi,

ndi kukonzeratu zovala ngati dothi;

17 azikonzeretu, koma wolungama adzazivala,

ndi wosalakwa adzagawa ndalamazo.

18 Amanga nyumba yake ngati kangaude,

ndi ngati wolindira amanga dindiro.

19 Agona pansi ali wachuma, koma saikidwa;

potsegula maso ake, wafa chikomo.

20 Zoopsa zimgwera ngati madzi;

nkuntho umtenga usiku.

21 Mphepo ya kum’mawa imtenga, nachoka iye;

nimkankha achoke m’malo mwake.

22 Pakuti Mulungu adzamponyera zoopsa, osamleka;

kuthawa akadathawa m’dzanja lake.

23 Anthu adzamuombera manja,

nadzamuimbira mluzu achoke m’malo mwake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/27-bd63e4d17d63827b5beea54c88b61219.mp3?version_id=1068—

Categories
YOBU

YOBU 28

1 Koma kuli mtapo wasiliva,

ndi malo a golide amene amuyenga.

2 Chitsulo achitenga m’nthaka,

ndi mkuwa ausungunula kumwala.

3 Munthu athawitsa mdima,

nafunafuna mpaka malekezero onse,

miyala ya mdima wa bii ndi ya mthunzi wa imfa.

4 Aboola mgodi posiyana patali pokhala anthu;

aiwalika ndi phazi lopitapo;

apachikika kutali ndi anthu, nalendewalendewa.

5 Kunena za nthaka, kuchokera momwemo mumatuluka chakudya,

ndi m’munsi mwake musandulizika ngati ndi moto.

6 Miyala yake ndiyo malo a safiro,

ndipo ili nalo fumbi lagolide.

7 Njira imeneyi palibe chiombankhanga chiidziwa;

lingakhale diso la kabawi losapenyapo.

8 Nyama zodzikuza sizinapondapo,

ngakhale mkango waukali sunapitapo.

9 Munthu atambasulira dzanja lake kumwala;

agubuduza mapiri kuyambira kumizu.

10 Asema njira pakati pa matanthwe,

ndi diso lake liona chilichonse cha mtengo wake.

11 Atseka mitsinje ingadonthe;

natulutsira poyera chobisikachi.

12 Koma nzeru, idzapezeka kuti?

Ndi luntha, malo ake ali kuti?

13 Munthu sadziwa mtengo wake;

ndipo silipezeka m’dziko la amoyo.

14 Pozama pakuti, Mwa ine mulibe;

ndi nyanja ikuti, Kwa ine kulibe.

15 Silipezeka ndi golide,

sayesapo siliva mtengo wake.

16 Sailinganiza ndi golide wa Ofiri,

ndi sohamu wa mtengo wake wapatali kapena safiro.

17 Golide ndi krustalo sizilingana nayo;

ndi kusinthana kwake,

siisinthanika ndi zisambiro za golide woyengetsa.

18 Korali kapena ngale sizikumbukikapo.

Mtengo wake wa nzeru uposa wa korali wofiira.

19 Topazi wa Kusi sufanana nayo,

sailinganiza ndi golide wolongosoka.

20 Koma nzeru ifuma kuti?

Ndi luntha, pokhala pake pali kuti?

21 Popeza pabisikira maso a zamoyo zonse,

pabisikiranso mbalame za m’mlengalenga.

22 Chionongeko ndi Imfa zikuti,

Tamva mbiri yake m’makutu mwathu.

23 Mulungu ndiye azindikira njira yake,

ndiye adziwa pokhala pake.

24 Pakuti apenyerera malekezero a dziko lapansi,

naona pansi pa thambo ponse;

25 pamene anaikira mphepo muyeso wake,

nayesera madzi miyeso;

26 pakuchitira mvula lamulo,

ndi njira yoyendamo mphezi ya bingu;

27 pamenepo anaiona nzeru, naifotokozera;

anaikonza, naisanthula.

28 Koma kwa munthu anati,

Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru;

ndi kupatukana nacho choipa ndiko luntha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/28-e038ea55e9281f6c3929e8f7b1f4b24b.mp3?version_id=1068—

Categories
YOBU

YOBU 29

Yobu alinganiza chikhalidwe chake chakale ndi tsoka latsopano, nalimbika kuti sanachite zotchulidwazi

1 Ndipo Yobu anaonjezanso mwambi wake, nati,

2 Ha! Ndikadakhala monga m’miyezi yapitayi,

monga m’masiku akundisunga Mulungu;

3 muja nyali yake inawala pamutu panga,

ndipo ndi kuunika kwake ndinayenda mumdima;

4 monga umo ndinakhala m’masiku anga olimba,

muja uphungu wa Mulungu unakhala pahema panga.

5 Muja Wamphamvuyonse akali nane pamodzi,

ndi ana anga anandizinga;

6 muja popondera ine padakhatamira ndi mafuta amkaka,

ndi thanthwe linanditsanulira mitsinje ya mafuta a azitona!

7 Muja ndinatuluka kunka kuchipata kumzinda,

muja ndinakonza pokhala panga kukhwalala,

8 anyamata anandiona nabisala,

okalamba anandinyamukira, nakhala chilili.

9 Akalonga anadziletsa kulankhula,

ndi kugwira pakamwa pao;

10 mau a omveka anali zii,

ndi lilime lao linamamatira kumalakalaka ao.

11 Pakuti pondimva ine khutu, linandidalitsa;

ndipo pondiona diso, linandichitira umboni.

12 Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakufuula;

mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.

13 Dalitso la iye akati atayike linandidzera,

ndi mtima wa mkazi wamasiye ndinauimbitsa mokondwera.

14 Ndinavala chilungamo, ndipo chinandivala ine;

chiweruzo changa chinanga mwinjiro ndi nduwira.

15 Ndinali maso a akhungu,

ndi mapazi a otsimphina.

16 Ndinali atate wa waumphawi;

ndi mlandu wa iye amene sindinamdziwe ndinafunsitsa.

17 Ndipo ndinathyola nsagwada ya wosalungama,

ndi kukwatula chogwidwa kumano kwake.

18 Pamenepo ndinati, Ndidzatsirizika m’chisa changa;

ndipo ndidzachulukitsa masiku anga ngati mchenga.

19 Muzu wanga watambalala kufikira kumadzi;

ndi mame adzakhala pa nthambi yanga usiku wonse.

20 Ulemu wanga udzakhala wosaguga mwa ine,

ndi uta wanga udzakhala wosalifuka m’dzanja mwanga.

21 Anthu anandimvera, nalindira,

nakhala chete, kuti ndiwapangire.

22 Nditanena mau anga sanalankhulenso,

ndi kunena kwanga kunawakhera.

23 Anandilindira ngati kulindira mvula,

nayasama pakamwa pao ngati kulira mvula ya masika.

24 Ndinawaseka akapanda kulimbika mtima;

ndipo sanagwetse kusangalala kwa nkhope yanga.

25 Ndinawasankhira njira yao ndi kukhala mkulu wao.

Ndinakhala ngati mfumu mwa ankhondo ake,

ngati wotonthoza ofedwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/29-61687a8946ef1c110c43364a7f10869e.mp3?version_id=1068—