1 Mtima wanga ulema nao moyo wanga,
ndidzadzilolera kudandaula kwanga,
ndidzalankhula pakuwawa mtima wanga.
2 Ndidzati kwa Mulungu, Musanditsutse;
mundidziwitse chifukwa cha kutsutsana nane.
3 Chikukomerani kodi kungosautsa,
kuti mupeputsa ntchito yolemetsa manja anu,
ndi kuti muwalira pa uphungu wa oipa?
4 Muli nao maso a thupi kodi?
Mupenya kodi monga umo apenyera munthu?
5 Masiku anu akunga masiku a munthu kodi,
zaka zanu zikunga masiku a munthu;
6 kuti mufunsa mphulupulu yanga,
ndi kulondola choipa changa;
7 chinkana mudziwa kuti sindili woipa,
ndipo palibe wakupulumutsa m’dzanja lanu?
8 Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu,
koma mufuna kundiononga.
9 Mukumbukire kuti mwandiumba ngati dothi;
ndipo kodi mudzandibwezera kufumbi?
10 Simunanditsanule kodi ngati mkaka,
ndi kundilimbitsa ngati mase?
11 Munandiveka khungu ndi mnofu,
ndi kundilumikiza mafupa ndi mitsempha.
12 Mwandipatsa moyo, ndi kundikomera mtima,
ndi masamalidwe anu anasunga mzimu wanga.
13 Koma izi munazibisa mumtima mwanu;
ndidziwa kuti ichi muli nacho.
14 Ndikachimwa mundipenya;
ndipo simudzandimasula mphulupulu yanga.
15 Ndikakhala woipa, tsoka ine;
ndikakhala wolungama, sindidzakweza mutu wanga;
ndadzazidwa ndi manyazi,
koma penyani kuzunzika kwanga.
16 Ndipo mutu wanga ukadzikweza, mundisaka ngati mkango;
mubweranso ndi kudzionetsera modabwitsa kwa ine.
17 Mundikonzeranso mboni zonditsutsa,
ndi kundichulukitsira mkwiyo wanu;
nkhondo yobwerezabwereza yandigwera.
18 Potero munandibadwitsa chifukwa ninji?
Mwenzi nditapereka moyo wanga, lisanandione diso.
19 Ndikadakhala monga ngati sindikadakhala;
akadanditenga pobadwapo kunka nane kumanda.
20 Masiku anga satsala owerengeka nanga? Lindani.
Bandilekani kuti nditsitsimuke pang’ono,
21 ndisanachoke kunka kumene sindikabweranso,
ku dziko la mdima ndi la mthunzi wa imfa.
22 Dziko la mdima bii ngati mdima wandiweyani,
dziko la mthunzi wa imfa losalongosoka,
kumene kuunika kukunga mdima.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/10-ce34da4f829e5495004bd59a6b8c1687.mp3?version_id=1068—