Categories
YESAYA

YESAYA 20

Chizindikiro chakuthyoka Ejipito ndi Etiopiya

1 Chaka chimene kazembe wa ku Asiriya anafika ku Asidodi, muja Sarigoni mfumu ya Asiriya anamtumiza iye, ndipo iye anamenyana ndi Asidodi, naugonjetsa.

2 Nthawi imeneyo Yehova ananena ndi Yesaya, mwana wa Amozi, nati, Muka numasule chiguduli m’chuuno mwako, nuchichotse, nuvule nsapato yako kuphazi lako. Ndipo iye anatero, nayenda maliseche, ndi wopanda nsapato.

3 Ndipo Yehova anati, Monga mtumiki wanga Yesaya wayenda maliseche ndi wopanda nsapato zaka zitatu, akhale chizindikiro ndi chodabwitsa kwa Ejipito ndi kwa Etiopiya;

4 momwemo mfumu ya Asiriya idzatsogolera kwina am’nsinga a Ejipito, ndi opirikitsidwa a Etiopiya, ana ndi okalamba, amaliseche ndi opanda nsapato, ndi matako osavala, kuti achititse manyazi Ejipito.

5 Ndipo iwo adzakhala ndi mantha ndi manyazi, chifukwa cha Kusi, amene anawatama, ndi Ejipito, amene anawanyadira.

6 Ndipo wokhala m’mphepete mwa nyanja muno adzati tsiku limenelo, Taonani, kuyembekeza kwathu kuli kotero, kumene ife tinathawira atithangate kupulumutsidwa kwa mfumu ya Asiriya, ndipo ife tidzapulumuka bwanji?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/20-009691b992b2e81676a43779cfe83fae.mp3?version_id=1068—

Categories
YESAYA

YESAYA 21

Aneneratu za kugwa kwa Babiloni

1 Katundu wa chipululu cha kunyanja. Monga akamvulumvulu a kumwera apitirira, kufumira kuchipululu kudziko loopsa.

2 Masomphenya ovuta aonetsedwa kwa ine; wogula malonda wonyenga amangonyenga, ndi wofunkha amangofunkha. Kwera Elamu iwe; zunguniza Mediya iwe; kuusa moyo kwake konse ndakutonthoza.

3 Chifukwa chake m’chuuno mwanga mwadzazidwa ndi zopota; zopweteka zandigwira ine monga zopweteka za mkazi pobala mwana; zowawa zindiweramitsa, makutu anga sangathe kumva; ndichita mantha sindingathe kuona.

4 Mtima wanga uguguda, mantha andiopsetsa ine; chizirezire chimene ndinachikhumba chandisandukira kunthunthumira.

5 Iwo akonza pa gome lodyera, aika alonda, adya, namwa; ukani, akalonga inu, dzozani mafuta chikopa.

6 Pakuti Ambuye atero kwa ine, Muka, ika mlonda anene chimene achiona;

7 ndipo pamene iye anaona khamu, amuna apakavalo awiriawiri, khamu la abulu, khamu langamira, iye adzamvetsera ndi khama mosamalitsa.

8 Ndipo iye anafuulitsa ngati mkango, Ambuye inu, ine ndiimabe pamwamba pa nsanja nthawi ya usana, ndipo ndiikidwa mu ulonda wanga usiku wonse;

9 ndipo taonani, kuno kulinkudza khamu la amuna, apakavalo awiriawiri. Ndipo iye anayankha nati, Babiloni wagwa, wagwa; ndi mafano onse osema a milungu yake asweka, nagwa pansi.

10 Kuomba kwanga nanga, ndi za pa dwale langa: chimene ine ndinachimva kwa Yehova wa makamu Mulungu wa Israele, ndanena kwa inu.

Aneneratu za kuonongeka kwa Duma

11 Katundu wa Duma. Wina aitana kwa ine kuchokera ku Seiri, Mlonda, nthawi yanji ya usiku? Mlonda, nthawi yanji ya usiku?

12 Mlonda anati, Kuli kucha, koma kukali usiku; mukafuna kufunsa, funsani, bwerani, idzani.

Za kuonongeka kwa Arabiya

13 Katundu wa pa Arabiya. M’nkhalango ya mu Arabiya mudzagona, inu makamu oyendayenda a Dedani.

14 Muchingamire akumva ludzu ndi madzi; okhala m’dziko la Tema ananka kukomana ndi othawa ndi chakudya chao.

15 Pakuti iwo anathawa malupanga, malupanga osololedwa, ndi mauta olifuka ndi nkhondo yovuta.

16 Pakuti Ambuye anatero kwa ine, Chisanapite chaka malinga ndi zaka za wolembedwa ntchito, ulemerero wonse wa Kedara udzagoma;

17 ndi otsala amauta, ngwazi za ana a Kedara zidzachepa, pakuti Yehova Mulungu wa Israele wanena.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/21-e8c016b132491e62a698be6420815038.mp3?version_id=1068—

Categories
YESAYA

YESAYA 22

Aneneratu za kumangidwa misasa Yerusalemu

1 Katundu wa chigwa cha masomphenya. Mwatani kuti mwakwera nonsenu pamatsindwi?

2 Iwe amene wadzala ndi zimfuu, mzinda waphokoso, mzinda wokondwa; ophedwa ako sanaphedwe ndi lupanga, sanafe m’nkhondo.

3 Olamulira ako onse athawa pamodzi, anamangidwa ndi amauta; opezedwa ako onse anamangidwa pamodzi, nathawira patali.

4 Chomwecho ndinati, Usandiyang’ane ine, ndilira ndi kuwawa mtima; usafulumire kunditonthoza ine, chifukwa cha kufunkhidwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga.

5 Pakuti nditsiku laphokoso, ndi lopondereza pansi, ndi lothetsa nzeru, lochokera kwa Ambuye, Yehova wa makamu, m’chigwa cha masomphenya, kugumuka kwa malinga, ndi kufuulira kumapiri.

6 Ndipo Elamu anatenga phodo, ndi magaleta a anthu ndi apakavalo; ndipo Kiri anaonetsa zikopa.

7 Ndipo panali kuti zigwa zako zosankhika zinadzala magaleta, ndi apakavalo anadzinika okha pachipata.

8 Ndipo Iye anachotsa chophimba cha Yuda; ndipo iwe unayang’ana tsiku limenelo pa zida za m’nyumba ya nkhalango.

9 Ndipo inu munaona kuti pa mzinda wa Davide panagumuka mipata yambiri; ndipo munasonkhanitsa pamodzi madzi a m’thamanda lakunsi.

10 Ndipo inu munawerenga nyumba zaYerusalemu, ndipo munagwetsa nyumba, kuti mumangire linga.

11 Inu munapanganso chosungamo madzi a thamanda lakale, pakati pa malinga awiri; koma inu simunamuyang’ane iye amene anachichita icho, ngakhale kusamalira iye amene analipanga kale.

12 Ndipo tsiku limenelo Ambuye, Yehova wa makamu, anaitana kulira, ndi kugwa misozi, ndi kumeta, ndikuvala chigudulim’chuuno;

13 koma taonani, kukondwa, ndi kusekerera, ndi kupha ng’ombe, ndi kupha nkhosa, ndi kudya nyama, ndi kumwa vinyo; tiyeni tidye ndi kumwa, chifukwa mawa tidzafa.

14 Ndipo Yehova wa makamu wadzivumbulutsa yekha m’makutu mwanga, Ndithu choipa chimenechi sichidzachotsedwa pa inu kufikira inu mudzafa, ati Ambuye, Yehova wa makamu.

Kulangidwa kwa Sebina, kukuzidwa kwa Eliakimu

15 Atero Ambuye, Yehova wa makamu, Muka, pita iwe kwa kapitao uyu, kwa Sebina woyang’anira nyumba, ndi kuti,

16 Uchitanji iwe kuno, ndimo ndani ali nawe kuno, kuti iwe wagoba manda kuno, ndi kudzigobera manda pamwamba, ndi kudzisemera mogonamo m’thanthwe.

17 Taona Yehova adzakuponya iwe zolimba, monga mwamuna wamphamvu, inde adzakufumbata zolimba.

18 Iye ndithu adzakuzunguza, ndi kukuponyaponya ngati mpira m’dziko lalikulu; kumeneko iwe udzafa, ndipo kumeneko kudzakhala magaleta a ulemerero wako, iwe wochititsa manyazi banja la mbuye wako.

19 Ndipo Ine ndidzakutulutsa iwe mu ntchito yako, ndi kukutsitsa iwe pokhala pako.

20 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti Ine ndidzaitana mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya:

21 ndipo ndidzamveka iye chovala chako, ndi kumlimbikitsa ndi lamba lako, ndipo ndidzapereka ulamuliro wako m’dzanja lake; ndipo iye adzakhala atate wa okhala mu Yerusalemu ndi a nyumba ya Yuda.

22 Ndipo ndidzaika mfungulo wa nyumba ya Davide paphewa pake, ndipo iye adzatsegula, ndipo palibe wina adzatseka, iye adzatseka ndipo palibe wina adzatsegula.

23 Ndipo ndidzamkhomera iye ngati chikhomo cholimba; ndipo iye adzakhala mpando wa ulemerero wa banja la atate wake.

24 Ndipo iwo adzapachika pa iye ulemerero wonse wa banja la atate wake, obadwa ndi ana, mbiya zonse zazing’ono, ngakhale zikho ndi aguda omwe.

25 Tsiku limenelo, ati Yehova wa makamu, chikhomo chokhomeredwa polimba udzasukusika; nudzaguluka, ndi kugwa, ndi katundu wopachikidwapo adzadulidwa; pakuti Yehova wanena.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/22-fbe0280094d14956ec95cb4a7ca80443.mp3?version_id=1068—

Categories
YESAYA

YESAYA 23

Kupasuka ndi kumangidwanso kwa Tiro

1 Katundu wa Tiro. Kuwani, inu ngalawa za Tarisisi; chifukwa wapasudwa, kulibenso nyumba, kulibe polowera; kuchokera kudziko la Kitimu kwavumbulutsidwa kwa iwo.

2 Khalani chete, inu okhala m’chisumbu; iwe amene anakudzazanso amalonda a ku Sidoni, opita m’nyanja.

3 Ndi pa nyanja zazikulu anapindula ndi mbeu za ku Sihori ndizo dzinthu za ku mtsinje; ndi kumeneko kunali msika waamitundu.

4 Khala ndi manyazi, iwe Sidoni; chifukwa nyanja yanena, linga la kunyanja, ndi kuti, Ine sindinamve zowawa, kapena kubala, kapena kulera anyamata, kapena kulera anamwali.

5 Pofika mbiriyo ku Ejipito, iwo adzamva kuwawa kwambiri pa mbiri ya Tiro.

6 Olokani inu, kunka ku Tarisisi, kuwani, inu okhala m’chisumbu.

7 Kodi umene ndi mzinda wanu wokondwa, wachikhalire kale lomwe, umene mapazi ake anaunyamula kunka nao kutali kukhalako?

8 Ndani wapanga uphungu uno pa Tiro, mudzi umene upereka akorona, amalonda ake ali akalonga, ogulitsa ake ali olemekezeka padziko lapansi?

9 Yehova wa makamu wapanga uphungu uwu, kuipitsa kunyada kwa ulemerero wonse, kupepula onse olemekezeka a m’dziko lapansi.

10 Pita pakati padziko lako monga mtsinje, iwe mwana wamkazi wa Tarisisi; palibenso lamba.

11 Iye watambasula dzanja lake panyanja, wagwedeza maufumu; Yehova walamulira Kanani za amalonda, kupasula malinga ake.

12 Ndipo Iye anati, Iwe sudzakondwanso konse, iwe namwali wovutidwa, mwanawamkazi wa Sidoni; uka, oloka kunka ku Kitimu; ngakhale kumeneko iwe sudzapumai.

13 Taonani, dziko la Ababiloni; anthu awa sakhalanso; Asiriya analiika ilo likhale la zilombo zokhala m’chipululu; iwo amanga nsanja zao, nagumula nyumba za mafumu ake; nalipasula.

14 Kuwani, inu ngalawa za Tarisisi; pakuti linga lanu lapasulidwa.

15 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti Tiro adzaiwalika zaka makumi asanu ndi awiri, malinga ndi masiku a mfumu imodzi; zitapita zaka makumi asanu ndi ziwirizo, chidzakhala kwa Tiro monga m’nyimbo ya mkazi wadama.

16 Tenga mngoli, yendayenda m’mzinda, iwe mkazi wadama, amene unaiwalika; imba zokoma, chulukitsa nyimbo, kuti ukumbukiridwe.

17 Ndipo padzali, zitapita zaka makumi asanu ndi awirizo, kuti Yehova adzazonda Tiro, ndipo iye adzabwerera kumphotho yake, nadzachita dama ndi maufumu onse a dziko lapansi, okhala kunja kuno.

18 Malonda ake ndi mphotho yake zidzakhala zopatulikira Yehova; sizidzasungidwa kapena kuikidwa; chifukwa malonda ake adzakhala kwa iwo, amene akhala pamaso pa Yehova, kuti adye mokwana, navale chaulemu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/23-895e7408269b2504c3f0dc79c907271d.mp3?version_id=1068—

Categories
YESAYA

YESAYA 24

Chilango cha Mulungu cha padziko la Israele, ndi padziko lonse lapansi

1 Taonani, Yehova apululutsa dziko, nalipasula, nalitembenuza dodolido, nabalalitsa okhalamo ake.

2 Ndipo padzakhala monga ndi anthu, moteronso ndi ansembe; monga ndi mtumiki, moteronso ndi mbuyake; monga ndi mdzakazi, moteronso ndi mbuyake wamkazi; monga ndi wogula, moteronso ndi wogulitsa; monga ndi wobwereka, moteronso ndi wombwereka; monga ndi wotenga phindu, moteronso ndi wombwezera phindu kwa iye.

3 Dziko lidzapululuka konse, ndi kupasulidwa ndithu; pakuti Yehova anenana mau amenewa.

4 Dziko lirira nilifota, dziko lilefuka nilifota, anthu omveka a padziko alefuka.

5 Dzikonso laipitsidwa ndi okhalamo ake omwe, chifukwa iwo alakwa pamalamulo nasinthanitsa malemba, nathyolachipanganocha nthawi zonse.

6 Chifukwa chake chitemberero chadya dziko, ndi amene akhala m’menemo apezedwa ochimwa, chifukwa chake okhalamo a padziko atenthedwa, ndipo anthu owerengeka atsala.

7 Vinyo watsopano alira, mpesa ulefuka, mitima yonse yokondwa iusa moyo.

8 Kusangalala kwa mangaka kwalekeka, phokoso la iwo amene asekera litha, kukondwa kwa mngoli kwalekeka.

9 Iwo sadzamwa vinyo ndi kuimba nyimbo; chakumwa chaukali chidzawawa kwa iwo amene achimwa.

10 Mzinda wosokonezeka wagwetsedwa pansi; nyumba zonse zatsekedwa, kuti asalowemo munthu.

11 Muli mfuu m’makwalala chifukwa cha vinyo; kukondwa konse kwadetsedwa, kusangalala kwa dziko kwatha.

12 M’mzinda mwatsala bwinja, ndi chipata chamenyedwa ndi chipasuko.

13 Chifukwa chake padzakhala chotero pakati padziko mwa anthu, ngati kugwedeza kwa mtengo waazitona, ngati khunkha la mphesa, pakutha masika ake.

14 Amenewa adzakweza mau ao, nadzafuula; chifukwa cha chifumu cha Yehova, iwo adzafuula zolimba panyanja.

15 Chifukwa chake lemekezani inu Yehova kum’mawa, ngakhale dzina la Yehova, Mulungu wa Israele, m’zisumbu za m’nyanja.

16 Kuchokera ku malekezero a dziko ife tamva nyimbo zolemekeza wolungama. Koma ine ndinati, Ndaonda ine, ndaonda ine, tsoka kwa Ine! Amalonda onyenga amangonyenga; inde ogulitsa onyenga apambana kunyenga.

17 Mantha ndi dzenje ndi msampha zili pa iwe, wokhala m’dziko.

18 Ndipo padzali, kuti iye amene athawa mbiri yoopsa, adzagwa m’dzenje; ndi iye amene atuluka m’kati mwa dzenje, adzakodwa mumsampha, pakuti mazenera a kuthambo atsegudwa, ndi maziko a dziko agwedezeka.

19 Dziko lapansi lasweka ndithu, dziko lapansi lasungunukadi, dziko lapansi lili kugwedezeka kopambana.

20 Dziko lapansi lidzachita dzandidzandi, ngati munthu woledzera, ndi kunjenjemera, ngati chilindo; ndi kulakwa kwake kudzalilemera, ndipo lidzagwa losaukanso.

21 Ndipo padzali tsiku limenelo, kuti Yehova adzazonda kumwamba khamu lakumwamba, ndi mafumu a dziko lapansi.

22 Ndipo iwo adzasonkhanitsidwa pamodzi, monga ndende zimasonkhanitsidwa m’dzenje, ndi kutsekeredwa m’kaidi, ndipo atapita masiku ambiri adzawazonda.

23 Pompo mwezi udzanyazitsidwa, ndi dzuwa lidzakhala ndi manyazi, pakuti Yehova wa makamu adzalamulira chaulemerero m’phiri laZiyoni, ndi muYerusalemu, ndi pamaso pa akuluakulu ake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/24-4102f916f0c33adcae3b5c4c5ed8d854.mp3?version_id=1068—

Categories
YESAYA

YESAYA 25

Nyimbo yakulemekeza chifundo cha Mulungu

1 Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga, ndidzakukuzani Inu, ndidzatamanda dzina lanu, chifukwa mwachita zinthu zodabwitsa, ngakhale zauphungu zakale, mokhulupirika ndi m’zoonadi.

2 Chifukwa Inu mwasandutsa mzinda muunda; mzinda walinga bwinja; nyumba ya alendo kuti isakhale mzinda; sudzamangidwa konse.

3 Chifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani Inu, mzinda wa mitundu yakuopsa udzakuopani Inu.

4 Chifukwa Inu mwakhala linga la aumphawi, linga la osowa m’kuvutidwa kwake, pobisalira chimphepo, mthunzi wa pa dzuwa, pamene kuomba kwa akuopsa kufanana ndi chimphepo chakuomba tchemba.

5 Monga kutentha m’malo ouma, Inu mudzaletsa phokoso la alendo; nyimbo ya akuopsa idzaletseka, monga mthunzi uletsa dzuwa.

6 Ndipo m’phiri limeneli Yehova wa makamu adzakonzera anthu ake onse phwando la zinthu zonona, phwando la vinyo wa pamitsokwe, la zinthu zonona za mafuta okhaokha, la vinyo wansenga wokuntha bwino.

7 Ndipo Iye adzaononga m’phiri limeneli chophimba nkhope chovundikira mitundu yonse ya anthu, ndi nsalu yokutaamitunduonse.

8 Iye wameza imfa kunthawi yonse; ndipo Ambuye Mulungu adzapukuta misozi pa nkhope zonse; ndipo chitonzo cha anthu ake adzachichotsa padziko lonse lapansi; chifukwa Yehova wanena.

9 Ndipo adzanena tsiku limenelo, Taonani, uyu ndiye Mulungu wathu; tamlindirira Iye, adzatipulumutsa; uyu ndiye Yehova, tamlindirira Iye, tidzakondwa ndi kusekerera m’chipulumutso chake.

10 Chifukwa m’phiri limeneli dzanja la Yehova lidzakhalamo, ndipo Mowabu adzaponderezedwa pansi m’malo ake, monga udzu uponderezedwa padzala.

11 Ndipo iye adzatambasula manja ake pakati pamenepo, monga wosambira atambasula manja ake posambira; koma Iye adzagwetsa pansi kunyada kwake, pamodzi ndi kunyenga kwa manja ake.

12 Ndipo linga la pamsanje la machemba ako Iye waligwetsa, naligonetsa pansi, nalifikitsa padothi, ngakhale pafumbi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/25-416977ead7ae23b08dab2880ac5803c0.mp3?version_id=1068—

Categories
YESAYA

YESAYA 26

Nyimbo yakulemekeza kutchinjiriza kwa Yehova

1 Tsiku limenelo adzaimba nyimbo imeneyi m’dziko la Yuda, Ife tili ndi mzinda wolimba; Iye adzaika chipulumutso chikhale machemba ndi malinga.

2 Tsegulani pazipata, kuti mtundu wolungama, umene uchita zoonadi, ulowemo.

3 Inu mudzasunga mtima wokhazikika mu mtendere weniweni, chifukwa ukukhulupirirani Inu.

4 Khulupirirani Yehova nthawi zamuyaya, pakuti mwa Ambuye Yehova muli thanthwe lachikhalire.

5 Chifukwa Iye watsitsira pansi iwo amene anakhala pamwamba, mzinda wa pamsanje; Iye wautsitsa, wautsitsira pansi; waugwetsa pansi pa fumbi.

6 Phazi lidzaupondereza pansi; ngakhale mapazi a aumphawi, ndi mapondedwe a osowa.

7 Njira ya wolungama ili njira yoongoka; Inu amene muli woongoka, mukonza njira ya wolungama.

8 Inde m’njira ya maweruziro anu, Yehova, ife talindira Inu; moyo wathu ukhumba dzina lanu, ndi chikumbukiro chanu.

9 Ndi moyo wanga ndinakhumba Inu usiku; inde ndi mzimu wanga wa mwa ine ndidzafuna Inu mwakhama; pakuti pamene maweruziro anu ali padziko lapansi, okhala m’dziko lapansi adzaphunzira chilungamo.

10 Ungayanje woipa, koma sadzaphunzira chilungamo; m’dziko la machitidwe oongoka, iye adzangochimwa, sadzaona chifumu cha Yehova.

11 Yehova, dzanja lanu litukulidwa, koma iwo saona; koma iwo adzaona changu chanu cha kwa anthu, nadzakhala ndi manyazi; inde moto udzamaliza adani anu.

12 Yehova, mudzatikhazikitsira mtendere; pakuti mwatigwirira ntchito zathu zonse.

13 Yehova Mulungu wathu, pamodzi ndi Inu Ambuye ena adatilamulira ife; koma mwa Inu nokha tidzatchula dzina lanu.

14 Iwo afa, atha, sadzakhalanso ndi moyo; ali mizimu, sadzauka; chifukwa chake Inu munawazonda, ndi kuwaononga, mwathetsa chikumbukiro chao chonse.

15 Mwachulukitsa mtundu, Yehova, mwachulukitsa mtundu; Inu mwalemekezeka, mwakuza malire onse a dziko.

16 Yehova, iwo adza kwa Inu movutika, iwo anathira pemphero, muja munalikuwalanga.

17 Monga ngati mkazi wokhala ndi pakati, amene nthawi yake yakubala yayandikira, amva zopweteka, ndi kufuula m’zowawa zake; momwemo takhala ife pamaso panu, Yehova.

18 Ife tinali ndi pakati, ife tinamva zopweteka, tafanana ngati tabala mphepo; sitinachite chipulumutso chilichonse padziko lapansi; ngakhale okhala m’dziko lapansi sanagwe.

19 Akufa anu adzakhala ndi moyo; mitembo yao idzauka. Ukani muimbe, inu amene mukhala m’fumbi; chifukwa mame ako akunga mame a pamasamba, ndipo dziko lapansi lidzatulutsa mizimu.

20 Idzani, anthu anga, lowani m’zipinda mwanu, nimutseke pamakomo panu; nimubisale kanthawi kufikira mkwiyo utapita.

21 Pakuti taonani, Yehova adza kuchokera kumalo ake kudzazonda okhala padziko lapansi, chifukwa cha kuipa kwao; dziko lidzavumbulutsa mwazi wake, ndipo silidzavundikiranso ophedwa ake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/26-3ec228fc2df11ddca7bcd007701d7186.mp3?version_id=1068—

Categories
YESAYA

YESAYA 27

Munda wampesa wa Yehova

1 Tsiku limenelo Yehova ndi lupanga lake lolimba ndi lalikulu ndi lamphamvu adzalangaLeviyataninjoka yothamanga, ndi Leviyatani njoka yopindikapindika; nadzapha ching’ona chimene chili m’nyanja.

2 Tsiku limenelo: munda wa mphesa wavinyo, imbani inu za uwo.

3 Ine Yehova ndiusunga uwo; ndidzauthirira madzi nthawi zonse; ndidzausunga usiku ndi usana, kuti angauipse.

4 Ndilibe ukali; ndani adzalimbanitsa lunguzi ndi minga ndi Ine kunkhondo? Ndiziponde ndizitenthe pamodzi.

5 Kapena mlekeni, agwire mphamvu zanga, nachite nane mtendere; inde, achite nane mtendere.

6 M’mibadwo ikudzayo Yakobo adzamera mizu; Israele adzaphuka ndi kuchita mphundu; ndipo iwo adzadzaza ndi zipatso padziko lonse lapansi.

7 Kodi Mulungu wakantha Yakobo, monga umo anawakanthira akumkanthawo? Kapena kodi iye waphedwa malinga ndi kuphedwa kwa iwo amene anaphedwa ndi iye?

8 Munalimbana naye pang’ono, pamene munamchotsa; wamchotsa iye kuomba kwake kolimba tsiku la mphepo yamlumbanyanja.

9 Chifukwa chake, mwa ichi choipa cha Yakobo chidzafafanizidwa, ndipo ichi ndi chipatso chonse chakuchotsa tchimo lake; pamene iye adzayesa miyala yonse ya guwa la nsembe, ngati miyala yanjeresa yoswekasweka, zifanizo ndi mafano a dzuwa sizidzaukanso konse.

10 Pakuti mzinda wotchingidwa uli pa wokha, mokhalamo mwa bwinja, ndi mosiyidwa ngati chipululu; mwanawang’ombe adzadya kumeneko, nadzagonako pansi, nadzamaliza nthambi zake.

11 Ponyala nthambi zake zidzathyoledwa; akazi adzafika, nazitentha ndi moto, pakuti ali anthu opanda nzeru; chifukwa chake Iye amene anawalenga sadzawachitira chisoni, ndi Iye amene anawaumba sadzawakomera mtima.

12 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti Yehova adzaomba tirigu wake, kuchokera madzi a nyanja, kufikira kumtsinje wa Ejipito, ndipo mudzakunkhidwa mmodzi, inu ana a Israele.

13 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, lipenga lalikulu lidzaombedwa; ndipo adzafika omwe akadatayika m’dziko la Asiriya, ndi opirikitsidwa a m’dziko la Ejipito; ndipo adzapembedza Yehova m’phiri lopatulika la paYerusalemu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/27-b66afe371a3df3f93dc9b0dbf015b481.mp3?version_id=1068—

Categories
YESAYA

YESAYA 28

Kulangidwa kwa Efuremu ndi Yuda chifukwa cha kuuma mtima kwao

1 Tsoka kwa korona wakunyada wa oledzera a Efuremu, ndi kwa duwa lakufota la ulemerero wake wokongola, limene lili pamutu paiwo, amene agwidwa ndi vinyo, m’chigwa cha nthaka yabwino.

2 Taonani, Ambuye ali ndi wina wamphamvu wolimba; ngati chimphepo cha matalala, mkuntho wakuononga, ngati namondwe wa madzi amphamvu osefukira, adzagwetsa pansi ndi dzanja lamphamvu.

3 Korona wakunyada wa oledzera a Efuremu adzaponderezedwa;

4 ndi duwa lakufota la ulemerero wake wokongola, limene lili pamutu pa chigwa cha nthaka yabwino, lidzakhala ngati nkhuyu yoyamba kucha malimwe asanafike; poiona wakupenya imeneyo, amaidya ili m’dzanja lake.

5 Tsiku limenelo Yehova wa makamu adzakhala korona wa ulemerero, ndi korona wokongola kwa anthu ake otsala:

6 ndipo adzakhala mzimu wa chiweruziro kwa oweruza milandu, ndi mphamvu kwa iwo amene abweza nkhondo pachipata.

7 Koma iwonso adzandima ndi vinyo, nasochera ndi chakumwa chaukali, wansembe ndimneneriadzandima ndi chakumwa chaukali, iwo amezedwa ndi vinyo, nasochera ndi chakumwa chaukali, adzandima popenya, naphunthwa poweruza.

8 Pakuti magome onse adzazidwa ndi masanzi ndi udyo, palibe malo okonzeka.

9 Kodi Mulungu adzaphunzitsa yani nzeru? Kodi Iye adzamvetsa yani uthengawo? Iwo amene aletsedwa kuyamwa, nachotsedwa pamawere?

10 Pakuti pali langizo ndi langizo, langizo ndi langizo; lamulo ndi lamulo, lamulo ndi lamulo; kuno pang’ono, uko pang’ono.

11 Iai, koma ndi anthu a milomo yachilendo, ndi a lilime lina, Iye adzalankhula kwa anthu awa;

12 amene ananena nao, Uku ndi kupuma, mupumitsa wolema, ndi apa ndi potsitsimutsa, koma iwo anakana kumva.

13 Chifukwa chake mau a Yehova adzakhala kwa iwo langizo ndi langizo, langizo ndi langizo; lamulo ndi lamulo, lamulo ndi lamulo; kuno pang’ono, uko pang’ono; kuti ayende ndi kugwa chambuyo, ndi kuthyoka, ndi kukodwa mumsampha, ndi kugwidwa.

14 Chifukwa chake imvani mau a Yehova, inu amuna amnyozo, olamulira anthu awa a muYerusalemu.

15 Chifukwa inu munati, Ife tapangana pangano ndi imfa, tavomerezana ndi kunsi kwa manda; pakuti mliri wosefukira sudzatifikira ife; pakuti tayesa mabodza pothawirapo pathu, ndi kubisala m’zonyenga;

16 chifukwa chake Ambuye Yehova atero, Taonani, ndiika muZiyonimwala wa maziko, mwala woyesedwa mwala wa pangodya, wa mtengo wake wokhazikika ndithu; wokhulupirira sadzafulumira.

17 Ndipo ndidzayesa chiweruziro chingwe choongolera, ndi chilungamo chingwe cholungamitsira chilili; ndipo matalala adzachotsa pothawirapo mabodza, ndi madzi adzasefukira mobisalamo.

18 Ndipo pangano lanu ndi imfa lidzathedwa, ndi kuvomerezana kwanu ndi kunsi kwa manda kudzalephereka; popita mliri woopsa udzakuponderezani pansi.

19 Nthawi zonse umapita, udzakutengani; chifukwa m’mawa ndi m’mawa udzapita, usana ndi usiku; ndipo kudzakhala kuopsa kokha, kumva mbiri yake.

20 Pakuti kama wafupika, munthu sangatambalale pamenepo; ndi chofunda chachepa, sichingamfikire.

21 Pakuti Yehova adzauka monga m’phiri la Perazimu, nadzakwiya monga m’chigwa cha Gibiyoni; kuti agwire ntchito yake, ntchito yake yachilendo, ndi kuti achite chochita chake, chochita chake chachilendo.

22 Tsono musakhale amnyozo, kuti nsinga zanu zingalimbe; pakuti Ambuye, Yehova wa makamu, wandimvetsa za chionongeko chotsimikizidwa padziko lonse lapansi.

23 Tcherani inu makutu, imvani mau anga; mverani, imvani kulankhula kwanga.

24 Kodi mlimi amalimabe kuti abzale? Kodi amachocholabe, ndi kuswa zibuma za nthaka?

25 Atakonza thyathyathya pamwamba pake, kodi safesa ponse mawere, ndi kumwazamwaza chitowe, nafesa tirigu m’mizere ndi barele m’malo ake osankhika, ndi mchewere m’maliremo?

26 Pakuti Mulungu wake amlangiza bwino namphunzitsa.

27 Pakuti sapuntha mawere ndi chopunthira chakuthwa, ngakhale kuzunguniza njinga ya galeta pachitowe; koma amakulunga mawere ndi munsi, naomba chitowe ndi chibonga.

28 Tirigu wa mkate aperedwa; pakuti samampuntha osaleka; ngakhale kuyendetsapo njinga ya galeta wake, ngakhale kumphwanya ndi ziboda za akavalo ake sapera.

29 Ichinso chifumira kwa Yehova wa makamu, uphungu wake uzizwitsa ndi nzeru yake impambana.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/28-5487f852b34953bf624e60b87346d1fc.mp3?version_id=1068—

Categories
YESAYA

YESAYA 29

Aneneratu za kulangidwa kwa Yuda wosakhulupirika, komanso za chipulumutso chake

1 Eya Ariyele, Ariyele, mzinda umene Davide anamangapo zithando! Onjezerani chaka ndi chaka; maphwando afikenso;

2 pamenepo ndidzasautsa Ariyele, ndipo padzakhala maliro ndi kulira; koma iye adzakhala kwa Ine monga Ariyele.

3 Ndipo ndidzamanga zithando kuzungulira iwe ponse, ndipo ndidzamanga linga ndi kuunjika miulu yakumenyanirana ndi iwe.

4 Ndipo iwe udzagwetsedwa pansi, nudzanena uli pansi, ndi kulankhula kwako kudzakhala pansi kotuluka m’fumbi; ndi mau ako adzakhala ngati a wina amene ali ndi mzimu wobwebweta, kuchokera pansi, ndi kulankhula kwako kudzakhala konong’ona kochokera m’fumbi.

5 Koma khamu la achilendo ako lidzafanana ndi fumbi losalala, ndi khamu la oopsa lidzakhala monga mungu wochokachoka; inde kudzaoneka modzidzimuka dzidzidzi.

6 Ndipo Yehova wa makamu adzamzonda ndi bingu, ndi chivomezi, ndi mkokomo waukulu, kamvulumvulu, ndi mkuntho, ndi lawi la moto wonyambita.

7 Ndipo khamu la mitundu yonse yomenyana ndi Ariyele, ngakhale yonse yomenyana naye ndi linga lake, ndi kumsautsa idzafanana ndi loto, masomphenya a usiku.

8 Ndipo kudzafanana ndi munthu wanjala, pamene alota, ndipo, taonani, akudya; koma auka, ndipo m’kati mwake muli zii; kapena monga munthu waludzu pamene alota, ndipo taonani, akumwa; koma auka ndipo taonani walefuka, ndipo m’kati mwake muli gwaa; momwemo lidzakhala khamu la mitundu yonse yomenyana ndi phiri laZiyoni.

9 Khalani ndi kudabwa; sangalalani ndi kukhala akhungu; iwo aledzera, koma si ndi vinyo, ali dzandidzandi; koma si ndi chakumwa chaukali.

10 Pakuti Yehova watsanulira pa inu mzimu wa tulo togonetsa, natseka maso anu, ndiwo aneneri; naphimba mitu yanu, ndiwo alauli.

11 Ndipo masomphenya onse akusandukirani mau a m’buku limatidwa ndi phula, limene anthu amapereka kwa wina wodziwa kuwerenga, nati, Werengani umu; koma ati, Sindingathe, chifukwa lamatidwa ndi phula;

12 ndipo buku laperekedwa kwa wosadziwa kuwerenga, ndi kuti, Werengani umu; koma ati, Ine sindinaphunzire.

13 Ndipo Ambuye anati, Popeza anthu awa ayandikira ndi Ine ndi m’kamwa mwao, nandilemekeza ndi milomo yao, koma mtima wao uli kutali ndi Ine, ndi mantha ao akundiopa Ine, ndi lamulo la anthu analiphunzira;

14 chifukwa chake, taonani, ndidzachitanso mwa anthu awa ntchito yodabwitsa, ngakhale ntchito yodabwitsa ndi yozizwitsa; ndipo nzeru ya anthu ao anzeru idzatha, ndi luntha la anthu ao ozindikira lidzabisika.

15 Tsoka kwa iwo amene afunitsa kubisira Yehova uphungu wao, ndi ntchito zao zili mumdima, ndipo amati ndani ationa ife? Ndani atidziwa ife?

16 Ozolitsa inu! Kodi woumba adzayesedwa ngati dothi; kodi chinthu chopangidwa chinganene za iye amene anachipanga, Iye sanandipange ine konse; kapena kodi chinthu choumbidwa chinganene za iye amene anachiumba, Iye alibe nzeru?

17 Kodi sikatsala kamphindi kakang’ono, ndipo Lebanoni adzasanduka munda wobalitsa, ndi munda wobalitsa udzayesedwa nkhalango?

18 Ndipo tsiku limenelo gonthi adzamva mau a m’buku, ndi maso akhungu adzaona potuluka m’zoziya ndi mumdima.

19 Ofatsanso kukondwa kwao kudzachuluka mwa Yehova, ndi aumphawi a mwa anthu adzakondwerera mwa Woyera wa Israele.

20 Pakuti woopsa wagoma, ndi wonyoza watha, ndi onse odikira zolakwa alikhidwa;

21 amene apalamulitsa munthu mlandu, namtchera msampha iye amene adzudzula pachipata, nambweza wolungama ndi chinthu chachabe.

22 Chifukwa chake Yehova amene anaombola Abrahamu, atero za banja la Yakobo: Yakobo sadzakhala ndi manyazi tsopano, ngakhale nkhope yake tsopano sidzagwa.

23 Koma pamene iye aona ana ake, ntchito ya manja anga, pakati pa iye, iwo adzayeretsa dzina langa; inde, iwo adzayeretsa Woyera wa Yakobo, nadzaopa Mulungu wa Israele.

24 Iwonso osochera mumzimu adzadziwa luntha, ndi iwo amene ang’ung’udza adzaphunzitsidwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/29-f9e058f7943a19467d09b4447a8c5db4.mp3?version_id=1068—