Categories
OWERUZA

OWERUZA 10

Tola ndi Yairi aweruza Israele

1 Atafa Abimeleki, anauka kupulumutsa Israele Tola mwana wa Puwa, mwana wa Dodo munthu wa Isakara; nakhala iye mu Samiri ku mapiri a Efuremu.

2 Ndipo anaweruza Israele zaka makumi awiri ndi zitatu, nafa, naikidwa mu Samiri.

3 Atafa iye, anauka Yairi Mgiliyadi, naweruza Israele zaka makumi awiri mphambu ziwiri.

4 Ndipo anali nao ana aamuna makumi atatu okwera pa ana a abulu makumi atatu, iwo ndipo anali nayo mizinda makumi atatu, otchedwa midzi ya Yairi, mpaka lero lino, ndiyo m’dziko la Giliyadi.

5 Nafa Yairi, naikidwa mu Kamoni.

Aisraele achimwira Mulungu nagonjetsedwa ndi Afilisti ndi Amoni

6 Ndipo ana a Israele anaonjeza kuchita choipa pamaso pa Yehova, natumikira Abaala, ndi Aasitaroti, ndi milungu ya Aramu, ndi milungu ya Sidoni, ndi milungu ya Mowabu, ndi milungu ya ana a Amoni, ndi milungu ya Afilisti; ndipo anamleka Yehova osamtumikira.

7 Pamenepo mkwiyo wa Yehova unayakira Israele, nawagulitsa m’dzanja la Afilisti, ndi m’dzanja la ana a Amoni.

8 Ndipo anaphwanya napsinja ana a Israele chaka chija, natero ndi ana onse a Israele okhala tsidya lija la Yordani m’dziko la Aamori, ndilo Giliyadi, zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu.

9 Ndipo ana a Amoni anaoloka Yordani kuthiranso nkhondo Yuda ndi Benjamini, ndi nyumba ya Efuremu; napsinjika kwambiri Israele.

10 Ndipo ana a Israele anafuula kwa Yehova ndi kuti, Takuchimwirani, popeza tasiya Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.

11 Ndipo Yehova anati kwa ana a Israele, Kodi sindinakupulumutsani kwa Aejipito ndi kwa Aamori, ndi kwa ana a Amoni, ndi kwa Afilisti?

12 Asidoni omwe, ndi Aamaleke, ndi Amaoni anakupsinjani. Pamenepo munafuula kwa Ine, ndipo ndinakupulumutsani m’dzanja lao.

13 Koma mwandisiya Ine ndi kutumikira milungu ina, chifukwa chake sindikupulumutsaninso.

14 Mukani ndi kufuulira kwa milungu munaisankha, ikupulumutseni nyengo ya kusauka kwanu.

15 Koma ana a Israele anati kwa Yehova, Tachimwa, mutichitire monga mwa zonse zikomera pamaso panu; komatu mutipulumutse lero lino, tikupemphani.

16 Pamenepo anachotsa milungu yachilendo pakati pao, natumikira Yehova; ndipo mtima wake unagwidwa chisoni chifukwa cha mavuto a Israele.

17 Ndipo ana a Amoni analalikiridwa, namanga misasa mu Giliyadi. Ndi ana a Israele anasonkhana namanga misasa ku Mizipa.

18 Ndipo anthu, akalonga a Giliyadi, ananenana wina ndi mnzake, Ndaniyo adzayamba kulimbana ndi ana a Amoni? Iye adzakhala mkulu wa onse okhala mu Giliyadi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/10-ad807ccb666eb2a5e36efb3d611467f0.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 11

Yefita alanditsa Israele

1 Yefita Mgiliyadi ndipo anali ngwazi yamphamvu, ndiye mwana wa mkazi wadama; koma Giliyadi adabala Yefita.

2 Ndipo mkazi wa Giliyadi anambalira ana aamuna; koma atakula ana aamuna a mkaziyo anampirikitsa Yefita, nanena naye, Sudzalandira cholowa m’nyumba ya atate wako; pakuti ndiwe mwana wa mkazi wina.

3 Pamenepo Yefita anathawa abale ake, nakhala m’dziko la Tobu; ndipo anyamata opanda pake anasonkhana kwa Yefita, natuluka naye pamodzi.

4 Ndipo kunali, atapita masiku, ana a Amoni anachita nkhondo ndi Israele,

5 ndipo kunatero, pamene ana a Amoni anathira nkhondo pa Israele, akulu a Giliyadi anamuka kutenga Yefita m’dziko la Tobu;

6 nati kwa Yefita, Tiye ukhale kazembe wathu kuti tilimbane ndi ana a Amoni.

7 Ndipo Yefita anati kwa akulu a Giliyadi, Simunandide kodi, ndi kundichotsa m’nyumba ya atate wanga? Ndipo mundidzeranji tsopano pokhala muli m’kusauka?

8 Ndipo akulu a Giliyadi ananena ndi Yefita, Chifukwa chake chakuti takubwerera tsopano ndicho kuti umuke nafe ndi kuchita nkhondo ndi ana a Amoni, nudzakhala mkulu wathu wa pa onse okhala mu Giliyadi.

9 Ndipo Yefita anati kwa akulu a Giliyadi, Mukandifikitsanso kwathu kuchita nkhondo ndi ana a Amoni, nakawapereka Yehova pamaso panga, ndidzakhala mkulu wanu kodi?

10 Ndipo akulu a Giliyadi anati kwa Yefita, Yehova ndiye wakumvera pakati pa ife, tikapanda kuchita monga momwe wanena.

11 Pamenepo Yefita anamuka ndi akulu a Giliyadi, ndipo anthu anamuika mkulu wao ndi mtsogoleri wao; ndipo Yefita ananena mau ake onse pamaso pa Yehova ku Mizipa.

12 Ndipo Yefita anatuma mithenga kwa mfumu ya ana a Amoni, ndi kuti, Ndi chiyani ndi inu ndi kuti mwandidzera kuthira nkhondo dziko langa?

13 Ndipo mfumu ya ana a Amoni inati kwa mithenga ya Yefita, Chifukwa Israele analanda dziko langa pakukwera iye kuchokera ku Ejipito, kuyambira Arinoni mpaka Yaboki, ndi mpaka Yordani; ndipo tsopano undibwezere maikowa mwamtendere.

14 Ndipo Yefita anatumanso mithenga kwa mfumu ya ana a Amoni;

15 nanena naye, Atero Yefita, Israele sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la ana a Amoni;

16 pakuti pakukwera iwo kuchokera ku Ejipito Israele anayenda m’chipululu mpaka Nyanja Yofiira, nafika ku Kadesi;

17 pamenepo Israele anatuma mithenga kwa mfumu ya Edomu, ndi kuti, Ndikupemphani ndipitire pakati padziko lanu; koma mfumu ya Edomu siinamvera. Natumanso kwa mfumu ya Mowabu; nayenso osalola; ndipo Israele anakhala mu Kadesi.

18 Pamenepo anayenda m’chipululu, naphazira dziko la Edomu, ndi dziko la Mowabu, nadzera kum’mawa kwa dziko la Mowabu, namanga misasa tsidya lija la Arinoni; osalowa malire a Mowabu, pakuti Arinoni ndi malire a Mowabu.

19 Ndipo Israele anatuma mithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, mfumu ya ku Hesiboni; nanena naye Israele, Tikupemphani tipitire pakati padziko lanu, kunka kwathu.

20 Koma Sihoni sanakhulupirire Israele kuti apitire pakati pa malire ake; koma Sihoni anamemeza anthu ake onse, namanga misasa ku Yahazi, nathira nkhondo Israele.

21 Ndipo Yehova Mulungu wa Israele anapereka Sihoni ndi anthu ake onse m’dzanja la Israele, ndipo anawakantha, ndi Israele, analandira cholowa chake, dziko lonse la Aamori, nzika za m’dziko lija.

22 Ndipo analandira akhale cholowa chao, malire onse a Aamori, kuyambira Arinoni mpaka Yaboki, ndi kuyambira chipululu mpaka Yordani.

23 Motero Yehova Mulungu wa Israele anaingitsa Aamori, pamaso pa anthu ake Israele, ndipo kodi liyenera kukhala cholowa chanu?

24 Chimene akulandiritsani Kemosi mulungu wanu, simuchilandira cholowa chanu kodi? Momwemo aliyense Yehova Mulungu wathu waingitsa pamaso pathu, zakezo tilandira cholowa chathu.

25 Ndipo tsopano kodi inu ndinu wabwino woposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu; anatengana konse ndi Israele iyeyu kodi, kapena kuchita nao nkhondo konse kodi?

26 Pokhala Israele mu Hesiboni ndi midzi yake, ndi mu Aroere ndi midzi yake ndi m’mizinda yonse yokhala m’mphepete mwa Arinoni zaka mazana atatu; munalekeranji kulandanso nthawi ija?

27 Potero sindinakuchimwirani ine, koma mundichitira choipa ndinu kundithira nkhondo; Yehova Woweruzayo, aweruze lero lino pakati pa ana a Israele ndi ana a Amoni.

28 Koma mfumu ya ana a Amoni sanamvere mau a Yefita anamtumizirawo.

Chowinda cha Yefita

29 Pamenepo mzimu wa Yehova unamdzera Yefita, napitira iye ku Giliyadi, ndi Manase, napitira ku Mizipa wa Giliyadi, ndi kuchokera ku Mizipa wa Giliyadi anapitira kwa ana a Amoni.

30 Ndipo Yefita anawindira Yehova chowinda, nati, Mukaperekatu ana a Amoni m’dzanja langa,

31 ndipo kudzali kuti chilichonse chakutuluka pakhomo pa nyumba yanga kudzakomana nane pakubweranso ine ndi mtendere kuchokera kwa ana a Amoni, chidzakhala cha Yehova, ndipo ndidzachipereka nsembe yopsereza.

32 Potero Yefita anapita kwa ana a Amoni kuwathira nkhondo; ndipo Yehova anawapereka m’dzanja lake;

33 nawakantha kuyambira ku Aroere mpaka ufika ku Miniti, ndiyo mizinda makumi awiri, ndi ku Abele-Keranimu, makanthidwe aakulu ndithu. Motero ana a Amoni anagonjetsedwa pamaso pa ana a Israele.

34 Pofika Yefita ku Mizipa kunyumba yake, taonani, mwana wake wamkazi anatuluka kudzakomana naye ndi malingaka ndi kuthira mang’ombe; ndipo iyeyu anali mwana wake mmodzi yekha, analibe mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.

35 Ndipo kunali, pakumuona anang’amba zovala zake, nati, Tsoka ine, mwana wanga, wandiweramitsa kwakukulu, ndiwe wa iwo akundisaukitsa ine; pakuti ndamtsegulira Yehova pakamwa panga ine, ndipo sinditha kubwerera.

36 Ndipo anati kwa iye, Atate wanga, mwamtsegulira Yehova pakamwa panu, mundichitire ine monga umo mudatulutsa mau pakamwa panu; popeza Yehova anakuchitirani inu chilango pa adani anu, pa ana a Amoni.

37 Ndipo anati kwa atate wake, Andichitire ichi, andileke miyezi iwiri, kuti ndichoke ndi kutsikira kumapiri, ndi kulirira unamwali wanga, ine ndi anzanga.

38 Nati iye, Muka. Namuuza amuke akakhale miyezi iwiri; namuka iye ndi anzake, nalirira unamwali wake pamapiri.

39 Ndipo kunali pakutha miyezi iwiri, anabwerera kwa atate wake amene anamchitira monga mwa chowinda chake anachiwinda; ndipo sanamdziwe mwamuna. Motero unali mwambo mu Israele,

40 kuti ana aakazi a Israele akamuka chaka ndi chaka kumliririra mwana wa Yefita wa ku Giliyadi, masiku anai pa chaka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/11-23113561ae659784b23e39b308ae2a3c.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 12

Efuremu aukira Yefita

1 Pamenepo amuna a Efuremu analalikidwa, napita kumpoto; nati kwa Yefita, Wapitiriranji kuthira nkhondo ana a Amoni, osatiitana ife timuke nawe? Tidzakutenthera nyumba yako ndi moto pamutu pako.

2 Ndipo Yefita anati kwa iwo, Ine ndi anthu anga tinatsutsana kwakukulu ndi ana a Amoni, koma pamene ndinakuitanani inu simunandipulumutse m’dzanja lao.

3 Ndipo pakuona ine kuti simundipulumutsa, ndinataya moyo wanga ndi kupita kwa ana a Amoni; ndipo Yehova anawapereka m’dzanja langa; mwakwereranji tsono lero lino kundichitira nkhondo?

4 Pamenepo Yefita anamemeza amuna onse a mu Giliyadi nalimbana naye Efuremu; ndipo amuna a Giliyadi anakantha Efuremu, chifukwa adati, Inu Agiliyadi ndinu akuthawa Efuremu, pakati pa Efuremu ndi pakati pa Manase.

5 Ndipo Agiliyadi anatsekereza madooko a Yordani a Efuremu; ndipo kunatero kuti, akati othawa a Efuremu, Ndioloke, amuna a Giliyadi anati kwa Iye, Ndiwe Mwefuremu kodi? Akati, Iai;

6 pamenepo anati kwa iye, Unene tsono Shiboleti; ndipo akati, Siboleti, osakhoza kutchula bwino, amgwira namupha padooko pomwe pa Yordani; ndipo anagwa a Efuremu nthawi ija, zikwi makumi anai mphambu ziwiri.

7 Ndipo Yefita anaweruza Israele zaka zisanu ndi chimodzi; nafa Yefita Mgiliyadi, naikidwa m’mzinda wina wa Giliyadi.

Oweruza Ibzani, Eloni, Abidoni

8 Ndi pambuyo pake Ibizani wa ku Betelehemu anaweruza Israele.

9 Ndipo anali nao ana aamuna makumi atatu; ndi ana aakazi makumi atatu anawakwatitsa kwina, natengera ana ake aamuna ana aakazi makumi atatu ochokera kwina. Ndipo anaweruza Israele zaka zisanu ndi ziwiri.

10 Nafa Ibizani naikidwa ku Betelehemu.

11 Ndi pambuyo pake Eloni Mzebuloni anaweruza Israele; naweruza Israele zaka khumi.

12 Nafa Eloni Mzebuloni naikidwa mu Ayaloni m’dziko la Zebuloni.

13 Ndi pambuyo pake Abidoni mwana wa Hilele wa ku Piratoni anaweruza Israele.

14 Ndipo anali nao ana aamuna makumi anai ndi zidzukulu zazimuna makumi atatu, akuyenda okwera pa ana a abulu makumi asanu ndi awiri; naweruza Israele zaka zisanu ndi zitatu.

15 Nafa Abidoni mwana wa Hilele wa ku Piratoni, naikidwa mu Piratoni m’dziko la Efuremu ku mapiri a Amaleke.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/12-8ae42bd01ecd024ad60e37df43b83a4a.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 13

Aisraele agonjera Afilisti; abadwa Samisoni

1 Ndipo ana a Israele anaonjeza kuchita choipa pamaso pa Yehova; nawapereka Yehova m’dzanja la Afilisti zaka makumi anai.

2 Ndipo panali munthu wina wa Zora wa banja la Adani, dzina lake ndiye Manowa; ndi mkazi wake analibe mwana, sanabale.

3 Ndipo mthenga wa Yehova anamuonekera mkaziyo nanena naye, Taona tsopano, ulibe mwana wosabala iwe; koma udzaima ndi kubala mwana wamwamuna.

4 Chifukwa chake udzisamalire, usamwe vinyo kapena choledzeretsa, nusadye chinthu chilichonse chodetsa;

5 pakuti taona, udzaima, nudzabala mwana wamwamuna; pamutu pake sipadzafika lumo; pakuti mwanayo adzakhalira kwa MulunguMnazirichibadwire; nadzayamba iye kupulumutsa Israele m’dzanja la Afilisti.

6 Pamenepo anadza mkaziyo, nanena ndi mwamuna wake ndi kuti, Wandidzera munthu wa Mulungu; maonekedwe ake ndiwo ngati maonekedwe a mthenga wa Mulungu oopsa ndithu; ndipo sindinamfunse uko achokera kapena sanandiuzenso dzina lake;

7 koma anati kwa ine, Taona, udzaima, ndi kubala mwana wamwamuna; ndipo tsopano usamwe vinyo kapena choledzeretsa, nusadye chilichonse chodetsa; pakuti mwanayo adzakhalira kwa Mulungu Mnaziri chibadwire mpaka tsiku la kufa kwake.

8 Pamenepo Manowa anapembedza Yehova, nati, Yehova, ndikupemphani, atidzerenso munthu wa Mulungu mudamtumayo, natilangize icho tizichitira mwanayo akadzabadwa.

9 Ndipo Mulungu anamvera mau a Manowa; ndi mthenga wa Mulungu anamdzeranso mkaziyo, pamene anali m’munda, mwamuna wake Manowa palibe.

10 Ndipo mkaziyo anafulumira nathamanga, nauza mwamuna wake, nanena naye, Taona, wandionekera munthu anandidzerayo tsiku lija.

11 Nanyamuka Manowa natsata mkazi wake, namdzera mwamuna uja, nanena naye, Kodi ndinu mwamuna uja munalankhula ndi mkaziyu? Ndipo anati, Ndine amene.

12 Nati Manowa, Achitike tsopano mau anu; koma makhalidwe ake a mwanayo ndi machitidwe ake adzatani?

13 Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa Manowa, Zonse ndinazinena ndi mkazi azisamalire.

14 Chilichonse chichokera kumpesa asadyeko, asamwe vinyo kapena choledzeretsa, kapena kudya chilichonse chodetsa; zonse ndinamlamulira azisunge.

15 Ndipo Manowa anati kwa mthenga wa Yehova, Tiloleni tikuchedwetseni kuti tikukonzereni mwanawambuzi.

16 Koma mthenga wa Yehova anati kwa Manowa, Ungakhale undichedwetsa, sindidzadya mkate wako; ndipo ukakonza nsembe yopsereza, uziipereka kwa Yehova. Pakuti Manowa sanadziwe kuti ndiye mthenga wa Yehova.

17 Ndipo Manowa anati kwa mthenga wa Yehova, Dzina lanu ndani, kuti, atachitika mau anu, tikuchitireni ulemu.

18 Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa iye, Ufunsiranji dzina langa, popeza lili lodabwitsa?

19 Pamenepo Manowa anatenga mwanawambuzi pamodzi ndi nsembe yaufa, nazipereka kwa Yehova pathanthwe; ndipo mthengayo anachita modabwitsa, ndi Manowa ndi mkazi wake ali chipenyere.

20 Pakuti kunali, pakukwera lawi la moto paguwa la nsembe kumwamba, mthenga wa Yehova anakwera m’lawi la paguwalo; ndi Manowa ndi mkazi wake ali chipenyere; nagwa iwowa nkhope zao pansi.

21 Ndipo mthenga wa Yehova sanaonekerenso kwa Manowa kapena kwa mkazi wake. Pamenepo anadziwa Manowa kuti ndiye mthenga wa Yehova.

22 Nati Manowa kwa mkazi wake, Tidzafa ndithu pakuti taona Mulungu.

23 Koma mkazi wake ananena naye, Yehova akadafuna kutipha, sakadalandira nsembe yopsereza ndi nsembe yaufa padzanja lathu, kapena kutionetsa izi zonse, kapena kutimvetsa zoterezi nthawi ino.

24 Ndipo mkaziyo anabala mwana wamwamuna namutcha dzina lake Samisoni; nakula mwanayo, Yehova namdalitsa.

25 Ndipo mzimu wa Yehova unayamba kumfulumiza mtima ku misasa ya Dani pakati pa Zora ndi Esitaoli.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/13-03726c0d6c23c8497e643c593cbc7fdb.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 14

Ukwati wa Samisoni

1 Ndipo Samisoni anatsikira ku Timna, naona mkazi wa ku Timna wa ana aakazi a Afilisti.

2 Nakwera iye, nauza atate wake ndi amai wake, nati, Ndapenya mkazi mu Timna wa ana aakazi a Afilisti; ndipo tsono munditengere uyu akhale mkazi wanga.

3 Koma atate wake ndi amai wake ananena naye, Kodi palibe mkazi mwa ana aakazi a abale ako, kapena mwa anthu a mtundu wanga onse, kuti wamuka kutenga mkazi wa Afilisti osadulidwawo? Nati Samisoni kwa atate wake, Nditengereni iye, pakuti andikonda pamaso panga.

4 Koma atate wake ndi amai wake sanadziwe kuti chidachokera kwa Yehova ichi; popeza analikufuna kutola chifukwa ndi Afilisti. Ndipo nthawi ija Afilisti analamulira Israele.

Samisoni apha mkango

5 Pamenepo anatsikira Samisoni, ndi atate wake ndi mai wake ku Timna, nadza ku minda yampesa ya Timna; ndipo taona, mwana wa mkango wakomana naye namdzumira.

6 Ndipo unamgwera iye kolimba mzimu wa Yehova, naung’amba monga akadang’amba mwanawambuzi, wopanda kanthu m’dzanja lake; koma sanauze atate wake kapena amai wake chimene adachichita.

7 Ndipo anatsika nakamba ndi mkazi, namkonda Samisoni pamaso pake.

8 Atapita masiku ndipo anabweranso kudzamtenga, napatuka iye kukaona mtembo wa mkango; ndipo taona, m’chitanda cha mkango munali njuchi zoundana, ndi uchi.

9 Ndipo anaufula ndi dzanja lake, nayenda, namadya alimkuyenda, nadza kwa atate wake ndi amai wake, nawapatsa, nadya iwo; koma sanawauze kuti adaufula uchiwo m’chitanda cha mkango.

Awaphera anthu mwambi

10 Ndipo atate wake anatsikira kwa mkazi; ndi Samisoni anakonzerapo madyerero; pakuti amatero anyamata.

11 Ndipo kunali, pamene anamuona, anabwera nao anzake makumi atatu akhale naye.

12 Nanena nao Samisoni, Mundilole ndikuphereni mwambi; mukanditanthauziratu uwu m’masiku asanuwa a madyerero, ndi kumasulira uwu, ndidzakupatsani malaya a nsalu yabafuta makumi atatu ndi zovala zosinthanitsa makumi atatu;

13 koma ngati simutha kunditanthauzira uwu mudzandipatsa ndinu malaya a nsalu yabafuta makumi atatu ndi zovala zosinthanitsa makumi atatu. Pamenepo ananena naye, Mwambi wako tiumve.

14 Ndipo ananena nao,

Chakudya chinatuluka m’mwini kudya,

ndi chozuna chinatuluka m’mwini mphamvu.

Ndipo masiku atatu sanakhoze kutanthauzira mwambiwo.

15 Koma kunali, tsiku lachisanu ndi chiwiri anati kwa mkazi wa Samisoni, Kopa mwamuna wako, atitanthauzire mwambiwo; tingatenthe iwe ndi nyumba ya atate wako ndi moto. Kodi mwatiitana kulanda zathu; si momwemo?

16 Ndipo mkazi wa Samisoni analira pamaso pake, nati, Ungondida, osandikonda; waphera anthu a mtundu wanga mwambi, osanditanthauzira ine. Ndipo ananena naye, Taona, sindinatanthauzire atate wanga kapena amai wanga, kodi ndikutanthauzire iwe?

17 Ndipo analira pamaso pake masiku asanu ndi awiriwo pochitika madyerero ao; koma kunali kuti tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuuza, popeza anamuumiriza; ndipo anatanthauzira anthu a mtundu wake mwambiwo.

18 Ndipo amuna a pamzinda anati kwa Samisoni tsiku lachisanu ndi chiwiri, lisanalowe dzuwa,

Chozuna choposa uchi nchiyani;

ndi champhamvu choposa mkango nchiyani?

Pamenepo ananena nao,

Mukadapanda kulima ndi ng’ombe yanga,

simukadatha kumasulira mwambi wanga.

19 Ndipo mzimu wa Yehova unamgwera Samisoni, natsikira iye kwa Asikeloni, nawakantha amuna makumi atatu, natenga zovala zao, nawapatsa omasulira mwambiwo zovala zosinthanitsa. Koma adapsa mtima, nakwera kunka kunyumba ya atate wake.

20 Ndipo mkazi wake wa Samisoni anakhala wa mnzake, amene adakhala bwenzi lake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/14-f7204f85e9f43d3d5265e3ea9e984b11.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 15

Samisoni atentha za m’minda ya Afilisti

1 Ndipo kunali atapita masiku, nyengo ya kucheka tirigu Samisoni anakacheza ndi mkazi wake ndi kumtengera mwanawambuzi, nati, Ndidzalowa kwa mkazi wanga kuchipinda. Koma atate wake sanamlole kulowamo.

2 Nati atate wake, Ndinanenetsa kuti umuda konse, potero ndinampereka kwa bwenzi lako; mng’ono wake sakoma koposa iye nanga? Ukhale naye, m’malo mwa winayu.

3 Koma Samisoni, ananena nao, Nthawi ino ndikhala wosapalamula pa Afilisti, powachitira choipa ine.

4 Namuka Samisoni, nagwira ankhandwe mazana atatu, natenga miuni, nalunza michira, naika muuni pakati pa michira iwiri iliyonse.

5 Nayatsa miuni, nawataya ku tirigu wosacheka wa Afilisti, natentha miulu, ndi tirigu wosacheka yemwe, ndi minda yaazitonayomwe.

6 Pamenepo Afilisti anati, Wachita ichi ndani? Nati, Samisoni mkamwini wa munthuyo wa ku Timna, popeza analanda mkazi wake, nampereka kwa mnzake. Pamenepo Afilisti anakwera namtentha mkaziyo ndi atate wake ndi moto.

7 Ndipo Samisoni ananena nao, Mukatero ndidzakubwezerani chilango ndi pamenepo ndidzaleka.

8 Ndipo anawakantha nyung’unyu ndi ntchafu, makanthidwe aakulu; natsika nakhala m’phanga mwa thanthwe la ku Etamu.

Ayesa kumanga Samisoni, napha iye anthu ambiri

9 Pamenepo Afilisti anakwera, namanga misasa mu Yuda, natandika mu Lehi.

10 Ndipo anthu a Yuda anati, Mwatikwerera chifukwa ninji? Nati iwo, Takwera kumanga Samisoni, kumchitira iye monga anatichitira ife.

11 Pamenepo anatsikira ku phanga la Etamu amuna zikwi zitatu a ku Yuda, nati kwa Samisoni, Sudziwa kodi kuti Afilisti ndiwo akutilamulira ife? Nchiyani ichi watichitira? Nati iye kwa iwowa, Monga anandichitira ine ndawachitira iwo.

12 Ndipo ananena naye, Tatsika ife tikumange, kuti tikupereke m’dzanja la Afilisti, Nanena nao Samisoni, Mundilumbirire kuti simudzandigwera nokha.

13 Ndipo anati kwa iye, Iai, koma kumanga tidzakumanga, ndi kukupereka m’dzanja lao; koma kupha sitikupha iwe. Nammanga iye ndi zingwe ziwiri zatsopano, nakwera naye kuchokera kuthanthwe.

14 Pamene anafika ku Lehi Afilisti anafuula pokomana naye; koma mzimu wa Yehova unamgwera kolimba, ndi zingwe zokhala pa manja ake zinanga thonje lopserera ndi moto, ndi zomangira zake zinanyotsoka pa manja ake.

15 Ndipo anapeza chibwano chatsopano cha bulu, natambasula dzanja lake nachigwira, nakantha nacho amuna chikwi chimodzi.

16 Nati Samisoni,

Ndi chibwano cha bulu, miulumiulu,

amuna chikwi ndawakantha ndi chibwano cha bulu.

17 Ndipo kunali, atatha kunena, anataya chibwano m’dzanja lake; nawatcha malowo Ramatilehi ndiko kunena chitunda cha chibwano.

18 Ndipo anamva ludzu lambiri, naitana kwa Yehova, nati, Mwapatsa Inu chipulumutso ichi chachikulu ndi dzanja la kapolo wanu; ndipo kodi ndife nalo ludzu tsopano ndi kugwa m’dzanja la osadulidwa awa?

19 Pamenepo Mulungu anang’amba pokumbika paja pa Lehi, natulukamo madzi; namwa iye, nubwera moyo wake, natsitsimuka iye; chifukwa chake anawatcha dzina lake, Kasupe wa wofuula, ndiwo mu Lehi mpaka lero lino.

20 Ndipo Samisoni anaweruza Israele m’masiku a Afilisti zaka makumi awiri.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/15-960a0e8fc743a979e2905ff9e7b34771.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 16

Samisoni ku Gaza

1 Ndipo Samisoni anamuka ku Gaza, naonako mkazi wadama, nalowana naye.

2 Koma wina anauza a ku Gaza, ndi kuti, Samisoni walowa kuno. Pamenepo anamzinga, namlalira usiku wonse pa chipata cha mzinda, nakhala chete usiku wonse ndi kuti, Tidikire mpaka kucha, pamenepo tidzamupha.

3 Koma Samisoni anagona mpaka pakati pa usiku, nauka pakati pa usiku, nagwira zitseko za pa chipata cha mzinda, ndi mphuthu ziwirizo, nazichotsa ndi mpiringidzo womwe, naziika pa mapewa ake, nakwera nazo pamwamba paphiri lili pandunji pa Hebroni.

Delila apereka Samisoni

4 Ndipo pambuyo pake kunali kuti anakonda mkazi m’chigwa cha Soreki, dzina lake ndiye Delila.

5 Ndipo akalonga a Afilisti anamkwerera mkaziyo, nanena naye, Umkope nuone umo muchokera mphamvu yake yaikulu, ndi umo tingakhoze kumtha khama, kuti timmange kumzunza; ndipo tidzakupatsa aliyense ndalama mazana khumi ndi limodzi.

6 Pamenepo Delila anati kwa Samisoni, Ndikupempha, undiuze umo muchokera mphamvu yako yaikulu, ndi chimene angakumange nacho, kuti akuzunze.

7 Nanena naye Samisoni, Akandimanga nazo nsinga zatsopano zisanu ndi ziwiri zosauma, ndidzakhala wofooka, wakunga munthu wina.

8 Pamenepo akalonga a Afilisti anakwera nazo kwa mkaziyo nsinga zatsopano zisanu ndi ziwiri zosauma; ndipo iye anammanga nazo.

9 Koma anali nao omlalira m’chipinda cha m’kati. Nanena naye, Afilisti akugwera, Samisoni. Pamenepo anadula nsingazi, monga iduka m’khosi yathonje pokhudza moto. M’mwemo mphamvu yake siinadziwike.

10 Pamenepo Delila anati kwa Samisoni, Taona, wandipusitsa, ndi kundiuza mabodza; undiuze tsopano, ndikupempha, chimene angakumange nacho.

11 Nanena naye, Akandimangitsa nazo zingwe zatsopano, zosagwira nazo ntchito pamenepo ndidzakhala wofooka wakunga munthu wina.

12 Ndipo Delila anatenga nsinga zatsopano, nammanga nazo, nanena naye, Afilisti akugwera, Samisoni. Ndi omlalira analikulinda m’chipinda cha m’kati. Koma anazidula pa manja ake ngati thonje.

13 Pamenepo Delila anati kwa Samisoni, Mpaka tsopano wandipusitsa, ndi kundiuza mabodza; undiuze chimene angakumange nacho. Nanena naye, Ukaomba njombi zisanu ndi ziwiri za pamutu panga mwa thonje loyala ndiko.

14 Ndipo anachimanga ndi phanga, nati kwa iye, Akugwera Afilisti, Samisoni; nagalamuka iye patulo take, nazula phanga la pamtanda, ndi thonje loyala lomwe.

15 Pamenepo ananena naye, Ukati bwanji, Ndikukonda, osamvana nane mtima wako? Wandipusitsa katatu tsopano, osandiuza umo muchokera mphamvu yako yaikulu.

16 Ndipo kunali, popeza anamuumiriza masiku onse ndi mau ake, namkakamiza, moyo wake unavutika nkufuna kufa.

17 Pomwepo anamfotokozera mtima wake wonse, nanena naye, Pamutu panga sipanapite lumo, pakuti ndineMnaziriwa Mulungu chiyambire mimba ya mai wanga; akandimeta, mphamvu yanga idzandichokera, ndidzakhala wofooka wakunga munthu wina aliyense.

18 Ndipo pamene Delila anaona kuti adamfotokozera mtima wake wonse, anatuma naitana akalonga a Afilisti, ndi kuti, Kwerani nthawi ino, pakuti wandifotokozera za mtima wake wonse. Nakwera akalonga a Afilisti nadza kwa iye nabwera nazo ndalamazo m’dzanja lao.

19 Pamenepo anamgonetsa pa mabondo ake, naitana munthu, nameta njombi zake zisanu ndi ziwiri; nayamba kumzunza, nimchokera mphamvu yake.

20 Ndipo anati, Afilisti akugwera, Samisoni. Nagalamuka iye m’tulo take, nati, Ndizituluka ngati nthawi zina, ndi kudzitakasika. Koma sanadziwe kuti Yehova adamchokera.

21 Pamenepo Afilisti anamgwira, namkolowola maso, natsika naye ku Gaza, nammanga ndi maunyolo amkuwa; namperetsa m’kaidi.

22 Koma atammeta tsitsi la pamutu pake linayamba kumeranso.

Samisoni agwetsa nyumba ya Dagoni, namwalira

23 Ndipo anasonkhana akalonga a Afilisti kuperekera Dagoni mulungu wao nsembe yaikulu, ndi kusekerera; pakuti anati, Mulungu wathu wapereka Samisoni mdani wathu m’dzanja lathu.

24 Ndipo pakumuona anthu analemekeza mulungu wao, pakuti anati, Mulungu wathu wapereka m’dzanja lathu mdani wathu, ndiye wakupasula dziko lathu, amene anatiphera ambiri.

25 Ndipo kunali, pakukondwera mitima yao, anati, Kaitaneni Samisoni, atisewerere. Naitana Samisoni m’kaidi; nasewera iye pamaso pao; ndipo anamuka iye pakati pa mizati.

26 Ndipo Samisoni anati kwa mnyamata womgwira dzanja, Ndileke, ndikhudze mizati imene nyumba ikhazikikapo, kuti nditsamirepo.

27 Koma nyumbayi inadzala ndi amuna ndi akazi; ndi akalonga onse a Afilisti anali momwemo ndi patsindwi panali amuna ndi akazi ngati zikwi zitatu akuyang’ana pakusewera Samisoni.

28 Pamenepo Samisoni anaitana kwa Yehova, nati, Yehova, Mulungu, mundikumbukire, ndikupemphani, ndi kundilimbitsa, ndikupemphani, nthawi ino yokha, Mulungu, kuti ndidzilipsiriretu tsopano apa Afilisti, chifukwa cha maso anga awiri.

29 Ndipo Samisoni anagwira mizati iwiri ya pakati imene nyumba inakhazikikapo, natsamirapo wina ndi dzanja lamanja, ndi unzake ndi dzanja lamanzere.

30 Nati Samisoni, Ndife nao Afilisti; nadziweramira mwamphamvu; ndipo nyumba idagwa pa akalonga, ndi pa anthu onse anali m’mwemo. Motero akufa amene anawapha pa kufa kwake anaposa amene anawapha akali moyo.

31 Pamenepo anatsika abale ake ndi banja lonse la atate wake, namnyamula, nakwera naye, namuika pakati pa Zora ndi Esitaoli, m’manda a Manowa atate wake. Ndipo adaweruza Israele zaka makumi awiri.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/16-4723bcd192e2e9ec1099fbb48dad071e.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 17

Mika ndi fano lake

1 Ndipo ku mapiri a Efuremu kunali munthu dzina lake ndiye Mika.

2 Ndipo iye anati kwa amai wake, Ndalama zija mazana khumi ndi limodzi anakuberani zimene munatembererapo, ndi kunenanso m’makutu mwanga, taonani ndalamazo ndili nazo, ndinazitenga ndine. Pamenepo amai wake anati, Yehova adalitse mwana wanga.

3 Nabwezera amake ndalama zija mazana khumi ndi limodzi; nati amai wake, Kupatula ndapatulira Yehova ndalamazo zichoke ku dzanja langa, zimuke kwa mwana wanga, kupanga nazo fano losema ndi fano loyenga; m’mwemo ndikubwezera izi.

4 Ndipo pamene anambwezera mai wake ndalamazo, mai wake anatapako ndalama mazana awiri, nazipereka kwa woyenga, ndiye anazipanga fano losema ndi fano loyenga; ndipo linakhala m’nyumba ya Mika.

5 Koma munthuyu Mika anali nayo nyumba ya milungu, napanga chovala cha wansembe, ndiaterafi, namninkha zansembe mwana wake wina wamwamuna, amene anakhala wansembe wake.

6 Masikuwa panalibe mfumu mu Israele, yense anachita chomuyenera m’maso mwake.

7 Ndipo panali mnyamata wa ku Betelehemu ku Yuda, wa banja la Yuda, ndiye Mlevi, nagonera iye komweko.

8 Adachokera munthuyo m’mudzi mu Betelehemu ku Yuda, kugonera paliponse akapeza pokhala; ndi pa ulendo wake anafika ku mapiri a Efuremu, kunyumba ya Mika.

9 Ndipo Mika ananena naye, Ufumira kuti? Nati kwa iye, Ndine Mlevi wa ku Betelehemu ku Yuda, ndilikumuka kugonera kumene ndikapeza pokhala.

10 Nanena naye Mika, Khalitsa nane, nukhale atate wanga, ndi wansembe wanga, ndipo ndidzakupatsa ndalama khumi pachaka, ndi chovala chofikira, ndi zakudya zako. Nalowa Mleviyo.

11 Ndi Mleviyo anavomera kukhalitsa ndi munthuyo; ndi mnyamatayo anamkhalira ngati mmodzi wa ana ake.

12 Ndipo Mika anamninkha zansembe Mleviyo, ndi mnyamatayo anakhala wansembe wake, nakhala m’nyumba ya Mika.

13 Nati Mika, Tsopano ndidziwa kuti Yehova adzandichitira chokoma, popeza ndili naye Mlevi akhale wansembe wanga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/17-59a84d5e6368e3c98c0f66ba33ef7c46.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 18

Ana a Dani alanda mafano a Mika

1 Masiku ajawo panalibe mfumu mu Israele; masiku ajanso fuko la Adani anadzifunira cholowa chakukhalako; pakuti kufikira tsiku lija sichinawagwere cholowa chao pakati pa mafuko a Israele.

2 Ndipo ana a Dani anatuma a banja lao amuna asanu a mwa iwo onse, anthu olimba mtima, a ku Zora, ndi a ku Esitaoli, kuzonda dziko ndi kufunafunamo; nanena nao, Mukani, mufunefune m’dziko. Nafika iwo ku mapiri a Efuremu kunyumba ya Mika, nagona komweko.

3 Pokhala iwo m’nyumba ya Mika, anazindikira mau a mnyamata Mleviyo, napatukirako, nanena naye, Anadza nawe kuno ndani? Uchitanji muno? Ukhala nacho chiyani kuno?

4 Ndipo ananena nao, Mika anandichitira chakutichakuti, napangana nane za ntchito, ndipo ndikhala wansembe wake.

5 Pamenepo ananena naye, Utifunsire kwa Mulungu, kuti tidziwe ngati ulendo wathu timukawo udzakoma.

6 Nanena nao wansembeyo, Mukani mumtendere, ulendo wanu muyendawo uli pamaso pa Yehova.

7 Pamenepo amuna asanuwa anachoka, nafika ku Laisi; naona anthu anali m’mwemo, kuti anakhala okhazikika mtima, monga anakhala Asidoni, odekha ndi osatekeseka; popeza m’dzikomo munalibe mwini bwalo wakuchititsa manyazi m’chinthu chilichonse; nasiyana kutali ndi Asidoni, ndipo analibe kanthu ndi munthu aliyense.

8 Ndipo asanuwo anafikanso kwa abale ao ku Zora ndi Esitaoli; ndi abale ao ananena nao, Mutani inu?

9 Nati iwo, Taukani, tiwakwerere; pakuti tapenya dziko, ndipo taonani, ndilo lokoma ndithu; ndi inu muli chete kodi? Musamachita ulesi kumuka ndi kulowa kulandira dzikolo.

10 Pomuka inu mudzafikira anthu okhazikika mtima ndi dziko lachitando; pakuti Mulungu walipereka m’dzanja lanu; pamenepo mposasowa kanthu kalikonse kali padziko lapansi.

11 Pamenepo amuna mazana asanu ndi limodzi, omangira zida za nkhondo m’chuuno, anaphumulako a banja la a Dani, anachokera ku Zora, ndi ku Esitaoli.

12 Nakwera namanga misasa mu Kiriyati-Yearimu, mu Yuda; chifukwa chake anatcha dzina lake la malowo chigono cha Dani, mpaka lero; taona, ali m’tseri mwa Kiriyati-Yearimu.

13 Ndipo anapitirira komweko kunka ku mapiri a Efuremu, nadza kunyumba ya Mika.

14 Pamenepo anayankha amuna asanu anamukawo kukazonda dziko la Laisi, nanena ndi abale ao, Kodi mudziwa kuti m’nyumba izi muli chovala cha wansembe, ndiaterafindi fano losema, ndi fano loyenga? Ndipo tsopano dziwani choyenera inu kuchita.

15 Napatuka iwo kunkako, nafika kunyumba ya mnyamata Mleviyo, ndiyo nyumba ya Mika, namfunsa ngati ali bwanji.

16 Ndipo amuna mazana asanu ndi limodzi omangira zida zao za nkhondo m’chuuno, ndiwo a ana a Dani, analikuima polowera pa chipata;

17 koma amuna asanu omukawo kukazonda dziko anakwera analowako, natenga fano losema, ndi chovala cha wansembe ndi aterafi, ndi fano loyenga; ndi wansembe anaima polowera pa chipata pamodzi ndi amuna mazana asanu ndi limodzi omangira zida za nkhondo m’chuuno.

18 Atalowa iwo m’nyumba ya Mika, natengako fano losema, chovala cha wansembe, ndi aterafi, ndi fano loyenga, wansembeyo ananena nao, Muchitanji?

19 Ndipo ananena naye, Khala chete, tseka pakamwa pako, numuke nafe, nutikhalire atate ndi wansembe wathu; chikukomera nchiti, kukhala wansembe wa nyumba ya munthu mmodzi, kapena kukhala wansembe wa fuko ndi banja mu Israele?

20 Nukondwera mtima wa wansembeyo, natenga iye chovala cha wansembe, ndi aterafi ndi fano losema, nalowa pakati pa anthu.

21 Atatero anabwerera, nachoka, natsogoza ana aang’ono ndi zoweta ndi akatundu.

22 Atafika kutali ndi nyumba ya Mika, Mikayo anawamemeza amuna a m’nyumba zoyandikizana ndi yake, natsata ndi kuwapeza ana a Dani.

23 Ndipo anafuula kwa ana a Dani. Nacheuka iwo nati kwa Mika, Chakusowa chiyani, kuti wamemeza anthu ako?

24 Nati iye, Mwanditengera milungu yanga ndinaipanga, ndi wansembe, ndi kuchoka; chinditsaliranso chiyani? Ndipo muneneranji kwa ine, Chakusowa nchiyani?

25 Koma ana a Dani anati kwa iye, Mau ako asamveke ndi ife, angakugwere anthu owawa mtima, nukataya moyo wako ndi wa iwo a m’nyumba mwako.

26 Nayenda ulendo wao ana a Dani; ndipo Mika pakuona kuti anamposa mphamvu, anatembenuka nabwerera kunyumba kwake.

27 M’mwemo anatenga zimene Mika adachipanga, ndi wansembe anali naye, nafika ku Laisi, kwa anthu odekha ndi okhazikika mtima, nawakantha ndi lupanga lakuthwa, natentha mzinda wao ndi moto.

28 Ndipo panalibe wolanditsa, popeza ku Sidoni nkutali, ndipo analibe kuyenderana ndi anthu ena; ndiko ku chigwa chokhala ku Beterehobu. Pamenepo anamanganso mzindawo, nakhala m’mwemo.

29 Ndipo analitcha dzina la mzindawo Dani, kutsata dzina la atate wao Dani wombala Israele; koma poyambapo dzina la mzinda linali Laisi.

30 Ndipo ana a Dani anadziimitsira fano losemalo; ndi Yonatani mwana wa Geresomo mwana wa Manase, iye ndi ana ake aamuna anali ansembe a fuko la Adani mpaka tsiku lija anatenga ndende anthu a m’dziko.

31 Motero anadziikira fano losema la Mika, limene adalipanga, masiku onse okhala nyumba ya Mulungu ku Silo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/18-e3d1443fc12d41753502508abe1853f2.mp3?version_id=1068—

Categories
OWERUZA

OWERUZA 19

Choopsa adachichita a ku Gibea

1 Ndipo kunali, masiku aja, pamene panalibe mfumu mu Israele, panali munthu Mlevi wogonera kuseri kwa mapiri a Efuremu amene anadzitengera mkazi wamng’ono wa ku Betelehemu ku Yuda.

2 Koma mkazi wake wamng’ono anachita chigololo akali naye, namchokera kunka kunyumba ya atate wake ku Betelehemu ku Yuda, nakhalako nthawi ya miyezi inai.

3 Koma anauka mwamuna wake namtsata kukamba naye zamtima, kumbwezanso; napita ndi mnyamata wake, ndi abulu awiri. Ndipo mkaziyo anadza naye kunyumba ya atate wake. Ndipo pakumuona atate wa mkaziyo anakondwera kukomana naye.

4 Ndipo mpongozi wake, ndiye atate wa mkaziyo, anamuimika kuti akhale naye masiku atatu; nadya namwa nagona komweko.

5 Ndipo kunali, tsiku lachinai, analawirira mamawa, nanyamuka iye kuchoka; koma atate wa mkaziyo anati kwa mkamwini wake, Limbitsa mtima wako ndi mkate pang’ono, ndipo utatero upite.

6 Nakhala pansi nadya namwa onse awiri pamodzi; nati kwa munthuyo atate wa mkaziyo, Uvomere, ugone kuno usiku, nusekerere mtima wako.

7 Ndipo munthuyo ananyamuka kuti amuke; koma mpongozi wakeyo anamkakamiza, nagonanso komweko.

8 Nalawirira mamawa tsiku lachisanu kuti amuke, koma atate wa mkaziyo anati, Ulimbitse mtima wako, nulindire lipendeke dzuwa; nadya iwo onse awiri.

9 Pamenepo munthuyo ananyamuka kuchoka, iye ndi mkazi wake wamng’ono ndi mnyamata wake; koma mpongozi wake, atate wa mkaziyo, ananena naye, Tapenya, lapendeka dzuwa, ugone kuno usiku; tapenya lapendekatu dzuwa, ugone kuno, nusekerere mtima wako; nimulawire mamawa kunka ulendo wanu kwanu.

10 Koma munthuyo anakana kugonako usiku, nanyamuka, nachoka, nadza pandunji pa Yebusi (ndiwoYerusalemu); ndi pamodzi naye panali abulu awiri omangirira mbereko; anali nayenso mkazi wake wamng’ono.

11 Pofika iwo pa Yebusi linalimkulowa dzuwa, ndi mnyamata anati kwa mbuye wake, Tiyeni, tipatukire mzinda uwu wa Ayebusi ndi kugona pomwepa.

12 Koma mbuye wake ananena naye, Tisapatukire mzinda wachilendo, wosati wa ana a Israele, koma tipitirire kunka ku Gibea.

13 Nati kwa mnyamata wake, Tiyeni, tiyandikire kwinako: tigone mu Gibea, kapena mu Rama.

14 Napitirira iwo, nayenda, ndi dzuwa linawalowera pafupi pa Gibea, ndiwo wa Benjamini.

15 Napatukirako, kuti alowe nagone ku Gibea; nalowa iye, nakhala pansi m’khwalala la mzindawo, pakuti panalibe wina wowalandira m’nyumba agonemo, wakuwapatsa pogona.

16 Ndipo taonani, munthu nkhalamba anachokera ku ntchito yake kumunda madzulo; munthuyu ndiye wa ku mapiri a Efuremu, nagonera ku Gibea; koma anthu pamenepo ndiwo Abenjamini.

17 Pamene anakweza maso ake anaona munthu wa pa ulendoyo m’khwalala la mzinda; ndi nkhalambayo inati, Umuka kuti? Ufumira kuti?

18 Ndipo ananena nayo, Tili kuchokera ku Betelehemu ku Yuda, kunka ku mbali za mapiri a Efuremu, ndiko ndifumira ine; koma ndidamuka ku Betelehemu ku Yuda; ndipo tsopano ndili kumuka kunyumba ya Yehova; koma palibe munthu wondipatsa nyumba.

19 Ngakhale udzu ndi chakudya cha abulu athu ziliko; ndi mkate ndi vinyo zilikonso kwa ine ndi kwa mdzakazi wako ndi kwa mnyamata wokhala ndi akapolo ako; kosasowa kanthu.

20 Ndipo nkhalambayo inati, Mtendere ukhale ndi iwe, komatu, zosowa zako zonse ndidzakupatsa ndi ine; pokhapo usagone m’khwalala.

21 Pamenepo anamlonga m’nyumba yake, napatsa abulu chakudya; ndipo iwo anasamba mapazi ao, nadya, namwa.

22 Pokondweretsa iwo mitima yao, taonani amuna a m’mzindawo, ndiwo anthu otama zopanda pake, anazinga nyumba, nagogodagogoda pachitseko; nati kwa mwini nyumba nkhalambayo ndi kuti, Tulutsa mwamunayo adalowa m’nyumba mwako kuti timdziwe.

23 Ndipo munthu mwini nyumba anawatulukira nanena nao, Iai, abale anga, musachite choipa chotere; popeza mwamuna uyu walowa m’nyumba mwanga, musachite chopusa ichi.

24 Taonani, mwana wanga wamkazi ndiye namwali, ndi mkazi wake wamng’ono siwa; ndiwatulutse iwo, muwachepetse iwo, ndi kuwachitira monga muyesa chokoma; koma mwamuna uyu musamchitire chopusa ichi.

25 Koma amunawo sanafune kumvera; motero munthuyu anagwira mkazi wake wamng’ono, natuluka naye kwa iwo kunja; namdziwa iwo, nachita naye zoipa usiku wonse mpaka m’mawa; namlola achoke mbandakucha.

26 Nadza mkaziyo, kutacha, nagwa pakhomo pa nyumba ya munthu padali mbuye wake, kufikira kutayera.

27 Pamene mbuye wake anauka mamawa, natsegula pakhomo pa nyumba, natuluka kunka ulendo wake, taona, mkazi wake wamng’ono, atagwa pakhomo pa nyumba ndi manja ake pachiundo.

28 Ndipo ananena naye, Tauka, timuke; koma panalibe womyankha. Pamenepo anamuika pabulu; nanyamuka mwamunayo, nanka kwao.

29 Ndipo pofika iye kunyumba kwake, anatenga mpeni, nagwira mkazi wake wamng’onoyo namgawa chiwalochiwalo magawo khumi ndi awiri, namtumiza ku malire onse a Israele.

30 Ndipo kunali kuti onse amene anachiona anati, Sichinachitika, inde sichinaoneke chotere chiyambire tsiku lokwera ana a Israele kutuluka m’dziko la Ejipito mpaka lero lino; lingiriranipo, mupangane nzeru, nimunene.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/19-6e5bd169203a5e74833554531f573c75.mp3?version_id=1068—