Categories
NUMERI

NUMERI Mau Oyamba

Mau Oyamba

Buku la

Numeri

likukamba za moyo wa ana a Israele pa zaka pafupi makumi anai, kuyambira pamene anachoka ku phiri la Sinai mpaka pamene anafika pafupi ndi Kanani chakum’mawa. Bukuli likutchedwa

Numeri

, kutanthauza “Kuwerengera”, chifukwa Mose adachita kalembera wa ana a Israele, asanachoke ku phiri la Sinai, nachitanso kalembera wina ku dziko la Mowabu pafupi ndi Yordani, patapita zaka ngati makumi anai.

Bukuli likuonetsa kuti Aisraele anali anthu amantha ndi otaya mtima msanga akakumana ndi zovuta, ndipo kawirikawiri adapandukira Mulungu naukiranso Mose amene Mulunguyo anamusankha kuti aziwatsogolera. Bukuli liwonetseranso kuleza mtima kwa Yehova ndi chifundo chake chosasinthika posamala anthu ake, ngakhale iwowo ankachirachimwira. Moseyo anali munthu woleza mtima, adakhala wokhulupirika kwa Mulungu ndi kwa anthu ake, nasenza udindo wake wofatsa ndi molimba mtima.

Za mkatimu

Aisraele asanachoke ku phiri la Sinai

1.1—9.23

a. Kalembera woyamba

1.1—4.9

b. Malangizo ndi malamulo osiyanasiyana

5.1—8.26

c. Paska wachiwiri

9.1-23

Ulendo wao kuchokera ku Sinai mpaka ku Mowabu

10.1—32.42

a. Afika ku malire a dziko la Kanani nakhala ku Kadesi

10.1—20.21

b. Atachoka ku Kadesi afika ku Mowabu

20.22—21.35

c. Zochitika zina ndi zina ku dziko la Mowabu

22.1—32.42

Mbiri mwachidule ya ulendo wao kuchokera ku Ejipito mpaka ku Mowabu

33.1-49

Awapatsa malangizo asanaoloke Yordani

33.50—36.13

Categories
NUMERI

NUMERI 1

Aisraele awerengedwa m’chipululu cha Sinai

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m’chipululu cha Sinai, m’chihema chokomanako, tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, chaka chachiwiri atatuluka m’dziko la Ejipito, ndi kuti,

2 Werenga khamu lonse la ana a Israele, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba ya makolo ao ndi kuwerenga maina ao, amuna onse mmodzimmodzi.

3 Iwe ndi Aroni muwawerenge monga mwa magulu ao, onse mu Israele akutuluka ku nkhondo, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu.

4 Ndipo pamodzi ndi inu pakhale munthu mmodzi wa mafuko onse; yense mkulu wa nyumba ya kholo lake.

5 Ndipo maina a amuna amene aime nanu ndi awa: wa Rubeni, Elizuri mwana wa Sedeuri.

6 Wa Simeoni, Selumiele mwana wa Zurishadai.

7 Wa Yuda, Nasoni mwana wa Aminadabu.

8 Wa Isakara, Netanele mwana wa Zuwara.

9 Wa Zebuloni, Eliyabu mwana wa Heloni.

10 Wa ana a Yosefe: wa Efuremu, Elisama mwana wa Amihudi; wa Manase, Gamaliele mwana wa Pedazuri.

11 Wa Benjamini, Abidani mwana wa Gideoni.

12 Wa Dani, Ahiyezere mwana wa Amisadai.

13 Wa Asere, Pagiyele mwana wa Okarani.

14 Wa Gadi, Eliyasafu mwana wa Deuwele.

15 Wa Nafutali, Ahira mwana wa Enani.

16 Iwo ndiwo oitanidwa a khamu, akalonga a mafuko a makolo ao; ndiwo akulu a zikwizo za Israele.

17 Ndipo Mose ndi Aroni anatenga anthu awa, onenedwa maina ao;

18 nasonkhanitsa khamu lonse tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, ndipo iwo anawakumbira magwero ao kutchula mabanja ao, ndi nyumba za makolo ao, ndi kuwerenga maina kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu mmodzimmodzi.

19 Monga Yehova analamula Mose, momwemo anawawerenga m’chipululu cha Sinai.

20 Ndipo ana a Rubeni, mwana woyamba wa Israele, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina mmodzimmodzi, amuna onse kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

21 owerengedwa ao a fuko la Rubeni, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu ndi chimodzi kudza mazana asanu.

22 A ana a Simeoni, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, owerengedwa ao, powerenga maina mmodzimmodzi, amuna onse kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

23 owerengedwa ao a fuko la Simeoni, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi zinai kudza mazana atatu.

24 A ana a Gadi, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

25 owerengedwa ao a fuko la Gadi, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu kudza mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu.

26 A ana a Yuda, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

27 owerengedwa ao a fuko la Yuda, ndiwo zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu zinai kudza mazana asanu ndi limodzi.

28 A ana a Isakara, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

29 owerengedwa ao a fuko la Isakara, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zinai kudza mazana anai.

30 A ana a Zebuloni, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

31 owerengedwa ao a fuko la Zebuloni, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana anai.

32 A ana a Yosefe, ndiwo a ana a Efuremu, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

33 owerengedwa ao a fuko la Efuremu, ndiwo zikwi makumi anai mphambu mazana asanu.

34 A ana a Manase, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

35 owerengedwa ao a fuko la Manase, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu ziwiri kudza mazana awiri.

36 A ana a Benjamini, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

37 owerengedwa ao a fuko la Benjamini, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu zisanu kudza mazana anai.

38 A ana a Dani, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

39 owerengedwa ao a fuko la Dani, ndiwo zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu ziwiri kudza mazana asanu ndi awiri.

40 A ana a Asere, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

41 owerengedwa ao a fuko la Asere, ndiwo zikwi makumi anai mphambu chimodzi kudza mazana asanu.

42 A ana a Nafutali, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo;

43 owerengedwa ao a fuko la Nafutali, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zitatu kudza mazana anai.

44 Iwo ndiwo amene anawerengedwa, amene Mose anawerenga pamodzi ndi Aroni, ndi akalonga a Israele, ndiwo amuna khumi ndi awiri; yense kunenera nyumba ya kholo lake.

45 Potero owerengedwa onse a ana a Israele monga mwa nyumba za makolo ao, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akutulukira kunkhondo mu Israele;

46 inde owerengedwa onse ndiwo zikwi mazana asanu ndi limodzi mphambu zitatu kudza mazana asanu ndi makumi asanu.

Alevi sawerengedwa

47 Koma Alevi monga mwa fuko la makolo ao sanawerengedwe mwa iwo.

48 Popeza Yehova adalankhula ndi Mose, ndi kuti,

49 Fuko la Levi lokha usaliwerenge, kapena kuona kufikira kwao mwa ana a Israele;

50 koma iwe, uike Alevi asunge chihema cha mboni, ndi zipangizo zake zonse, ndi zonse ali nazo; azinyamula chihema, ndi zipangizo zake zonse; namtumikire, namange mahema ao pozungulira pa chihema.

51 Ndipo akati amuke nacho chihemacho, Alevi amgwetse, ndipo akati achimange, Alevi achiimike; ndipo mlendo akayandikizako amuphe.

52 Ndipo ana a Israele amange mahema ao, yense ku chigono chake, ndi yense ku mbendera yake, monga mwa makamu ao.

53 Koma Alevi amange mahema ao pozungulira pa chihema cha mboni, kuti mkwiyo ungagwere khamu la ana a Israele; ndipo Alevi azidikira chihema cha mboni.

54 Momwemo ana a Israele anachita monga mwa zonse Yehova adauza Mose; anachita momwemo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/1-d43daa1e3239b923d40c0e039489e9d6.mp3?version_id=1068—

Categories
NUMERI

NUMERI 2

Malongosoledwe a chigono

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

2 Ana a Israele azimanga mahema ao yense ku mbendera yake, ya chizindikiro cha nyumba ya kholo lake; amange mahema ao popenyana ndichihema chokomanakopozungulira.

3 Ndipo iwo akumanga mahema ao ku m’mawa kotuluka dzuwa ndiwo a mbendera ya chigono cha Yuda, monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana Yuda ndiye Nasoni mwana wa Aminadabu.

4 Ndipo khamu lake, ndi owerengedwa ao, ndiwo zikwi makumi asanu ndi awiri, mphambu zinai, kudza mazana asanu ndi limodzi.

5 Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a fuko la Isakara; ndipo kalonga wa ana a Isakara ndiye Netanele mwana wa Zuwara.

6 Ndipo khamu lake, ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zinai kudza mazana anai.

7 Ndi fuko la Zebuloni: kalonga wa ana a Zebuloni ndiye Eliyabu mwana wa Heloni.

8 Ndi khamu lake, ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana anai.

9 Owerengedwa onse a chigono cha Yuda ndiwo zikwi makumi khumi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza zisanu ndi chimodzi mphambu mazana anai, monga mwa makamu ao. Ndiwo azitsogolera ulendo.

10 Mbendera ya chigono cha Rubeni ikhale kumwera monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Rubeni ndiye Elizuri mwana wa Sedeuri.

11 Ndi khamu lake, ndi olembedwa ake, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu ndi chimodzi kudza mazana asanu.

12 Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a fuko la Simeoni; ndi kalonga wa ana a Simeoni ndiye Selumiele mwana wa Zurishadai.

13 Ndi khamu lake ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi zinai kudza mazana atatu.

14 Ndi fuko la Gadi; kalonga wa ana a Gadi ndiye Eliyasafu mwana wa Reuwele.

15 Ndi khamu lake, ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu kudza mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu.

16 Owerengedwa onse a chigono cha Rubeni ndiwo zikwi makumi khumi mphambu makumi asanu ndi chimodzi kudza mazana anai mphambu makumi asanu, monga mwa makamu ao. Ndiwo azitsatana nao otsogolerawo.

17 Pamenepo khamu la Alevi azimuka nacho chihema chokomanako, pakati pa makamu; monga amamanga mahema ao, momwemo azimuka ulendo wao, munthu yense pamalo pake, monga mwa mbendera zao.

18 Mbendera ya chigono cha Efuremu izikhala kumadzulo monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Efuremu ndiye Elisama mwana wa Amihudi.

19 Ndi khamu lake, ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi anai kudza mazana asanu.

20 Ndipo oyandikizana naye ndiwo a fuko la Manase; ndi kalonga wa ana a Manase ndiye Gamaliele mwana wa Pedazuri.

21 Ndi khamu lake, ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu ziwiri kudza mazana awiri.

22 Ndi fuko la Benjamini: kalonga wa ana a Benjamini ndiye Abidani mwana wa Gideoni.

23 Ndi khamu lake, ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu zisanu kudza mazana anai.

24 Owerengedwa onse a chigono cha Efuremu ndiwo zikwi makumi khumi mphambu zisanu ndi zitatu kudza zana limodzi, monga mwa makamu ao. Iwo ndiwo aziyenda gulu lachitatu paulendo.

25 Mbendera ya chigono cha Dani izikhala kumpoto monga mwa makamu ao; ndi kalonga wa ana a Dani ndiye Ahiyezere mwana wa Amisadai.

26 Ndi khamu lake, ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu ziwiri kudza mazana asanu ndi awiri.

27 Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a fuko la Asere; ndi kalonga wa ana a Asere ndiye Pagiyele mwana wa Okarani.

28 Ndi khamu lake, ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi anai mphambu chimodzi kudza mazana asanu.

29 Ndi fuko la Nafutali: ndi kalonga wa ana a Nafutali ndiye Ahira mwana wa Enani.

30 Ndi khamu lake, ndi owerengedwa ake, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zitatu kudza mazana anai.

31 Owerengedwa onse a chigono cha Dani ndiwo zikwi makumi khumi mphambu makumi asanu kudza zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu ndi limodzi. Iwo ndiwo aziyenda m’mbuyo paulendo, monga mwa mbendera zao.

32 Amenewo ndiwo anawerengedwa a ana a Israele monga mwa nyumba za makolo ao; owerengedwa onse a m’zigono, monga mwa makamu ao, ndiwo zikwi makumi khumi kasanu ndi kamodzi mphambu zitatu kudza mazana asanu ndi makumi asanu.

33 Koma sanawerenge Alevi mwa ana a Israele; monga Yehova adauza Mose.

34 Ndipo ana a Israele anachita monga mwa zonse Yehova adauza Mose, momwemo anamanga mahema ao pa mbendera zao, momwemonso anayenda paulendo, yense monga mwa mabanja ake, monga mwa nyumba za makolo ake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/2-05704bd6f842bddd0414f7ff95506a7a.mp3?version_id=1068—

Categories
NUMERI

NUMERI 3

Ntchito ya Alevi

1 Mibadwo ya Aroni ndi Mose, tsiku lija Yehova ananena ndi Mose m’phiri la Sinai, ndi iyo.

2 Ndipo maina ao a ana aamuna a Aroni ndi awa: Woyamba Nadabu, ndi Abihu, Eleazara, ndi Itamara.

3 Awa ndi maina a ana aamuna a Aroni, ansembe odzozedwawo, amene anawadzaza manja ao achite ntchito ya nsembe.

4 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamaso pa Yehova muja anabwera nao moto wachilendo pamaso pa Yehova, m’chipululu cha Sinai, ndipo analibe ana; koma Eleazara ndi Itamara anachita ntchito ya nsembe pamaso pa atate wao Aroni.

5 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

6 Sendera nalo kuno fuko la Levi, ndi kuwaika pamaso pa Aroni wansembe, kuti amtumikire.

7 Ndipo azisunga udikiro wake, ndi udikiro wa khamu lonse pa khomo lachihema chokomanako, kuchita ntchito ya Kachisi.

8 Ndipo asunge zipangizo zonse za chihema chokomanako, ndi udikiro wa ana a Israele, kuichita ntchito ya Kachisi.

9 Ndipo uzipereka Alevi kwa Aroni ndi kwa ana ake aamuna; apatsidwa kwa iye ndithu, ochokera kwa ana a Israele.

10 Koma uike Aroni ndi ana ake aamuna, azisunga ntchito yao ya nsembe; ndi mlendo wakusendera pafupi amuphe.

11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

12 Ndipo taonani, Ine ndatenga Alevi kuwachotsa pakati pa ana a Israele m’malo mwa ana oyamba onse, oyamba kubadwa mwa ana a Israele; ndipo Aleviwo ndi anga.

13 Pakuti ana oyamba onse ndi anga; tsiku lija ndinakantha ana oyamba onse m’dziko la Ejipito ndinadzipatulira ana oyamba onse mu Israele, kuyambira munthu kufikira choweta; ndiwo anga; Ine ndine Yehova.

14 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m’chipululu cha Sinai, nati

15 Werenga ana a Levi monga mwa nyumba ya makolo ao, monga mwa mabanja ao; uwawerenge mwamuna yense wa mwezi umodzi ndi mphambu.

16 Ndipo Mose anawawerenga monga mwa mau a Yehova, monga adamuuza.

17 Ndipo ana a Levi maina ao ndi awa: Geresoni, ndi Kohati ndi Merari.

18 Ndi ana a Geresoni maina ao ndi awa, monga mwa mabanja ao: Libini, ndi Simei.

19 Ndi ana a Kohati monga mwa mabanja ao: Amuramu ndi Izihara, Hebroni ndi Uziyele.

20 Ndi ana a Merari monga mwa mabanja ao: Mali ndi Musi. Awa ndi mabanja a Alevi monga mwa nyumba za makolo ao.

21 Banja la Libini, ndi mabanja a Simei, ndiwo a Geresoni; ndiwo mabanja a Geresoni.

22 Owerengedwa ao, powawerenga amuna onse, kuyambira mwana wa mwezi umodzi ndi mphambu, owerengedwa ao ndiwo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu.

23 Mabanja a Ageresoni azimanga mahema ao pambuyo pa chihema kumadzulo.

24 Ndipo kalonga wa nyumba ya makolo a Ageresoni ndiye Eliyasafu mwana wa Laele.

25 Ndipo udikiro wa ana a Geresoni m’chihema, chokomanako ndiwo Kachisi, ndi chihema, chophimba chake, ndi nsalu yotsekera pa khomo la chihema chokomanako,

26 ndi nsalu zotchinga za kubwalo, ndi nsalu yotsekera pa chipata cha pabwalo, lokhala ku chihema, ndi ku guwa la nsembe pozungulira, ndi zingwe zake za ku ntchito zake zonse.

27 Banja la Aamuramu, ndi banja la Aizihara, ndi banja la Ahebroni, ndi banja la Auziyele ndiwo a Kohati; ndiwo mabanja a Akohati.

28 Powawerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu mphambu mazana asanu ndi limodzi, akusunga udikiro wa pamalo opatulika.

29 Mabanja a ana a Kohati azimanga mahema ao pa mbali ya chihema cha kumwera.

30 Ndipo kalonga wa nyumba ya makolo ao ya mabanja a Akohati ndiye Elizafani mwana wa Uziyele.

31 Ndipo udikiro wao ndiwo likasa, ndi gome, ndi choikaponyali, ndi maguwa a nsembe, ndi zipangizo za malo opatulika zimene achita nazo, ndi nsalu yotchinga, ndi ntchito zake zonse.

32 Ndipo kalonga wa akalonga a Alevi ndiye Eleazara mwana wa Aroni wansembeyo; ndiye aziyang’anira osunga udikiro wa pamalo opatulika.

33 Banja la Amali, ndi banja la Amusi ndiwo Amerari; ndiwo mabanja a Merari.

34 Ndipo owerengedwa ao, powerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu, ndiwo zikwi zisanu ndi chimodzi kudza mazana awiri.

35 Ndi kalonga wa nyumba ya makolo ya mabanja la Merari ndiye Zuriyele mwana wa Abihaili; azimanga mahema ao pa mbali ya chihema cha kumpoto.

36 Ndipo choyang’anira iwo, udikiro wao wa ana a Merari ndiwo matabwa a chihema, ndi mitanda yake, ndi mizati ndi nsanamira zake, ndi makamwa ake, ndi zipangizo zake zonse, ndi ntchito zake zonse;

37 ndi nsichi za pabwalo pozungulira, ndi makamwa ake, ndi zichiri zake, ndi zingwe zake.

38 Ndipo amene adamanga mahema ao pa khomo la Kachisi, kum’mawa, pa khomo la chihema chokomanako kotulukira dzuwa, ndiwo Mose ndi Aroni, ndi ana ake aamuna, akusunga udikiro wa malo opatulika, ndiwo udikiro wa ana a Israele; koma mlendo wakuyandikizako amuphe.

39 Owerengedwa onse a Alevi, adawawerenga Mose ndi Aroni, powauza Yehova, monga mwa mabanja ao, amuna mphambu, ndiwo zikwi makumi awiri mphambu ziwiri.

40 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Werenga amuna oyamba kubadwa onse a ana a Israele kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu nuone chiwerengo cha maina ao.

41 Ndipo unditengere Ine Alevi (Ine ndine Yehova) m’malo mwa oyamba kubadwa onse mwa ana a Israele; ndi ng’ombe za Alevi m’malo mwa zoyamba kubadwa zonse mwa ng’ombe za ana a Israele.

42 Ndipo Mose anawawerenga, monga Yehova adamuuza, oyamba kubadwa onse mwa ana a Israele.

43 Ndipo amuna onse oyamba kubadwa, powerenga maina, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu, owerengedwa ao, ndiwo zikwi makumi awiri mphambu ziwiri kudza mazana awiri ndi makumi asanu ndi awiri mphambu atatu.

44 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

45 Landira Alevi m’malo mwa oyamba kubadwa onse mwa ana a Israele, ndi ng’ombe za Alevi m’malo mwa ng’ombe zao; ndipo Alevi azikhala anga; Ine ndine Yehova.

46 Kunena za mazana awiri ndi makumi asanu ndi awiri kudza atatuwo oyamba kubadwa a ana a Israele, akuposa Alevi, akaomboledwe,

47 ulandire masekeli asanu pa munthu mmodzi; uwalandire pa muyeso wa sekeli wa malo opatulika (sekeli ndiwo magera makumi awiri);

48 nupereke ndalama zimene akuposawo anaomboledwa nazo kwa Aroni ndi kwa ana ake aamuna.

49 Pamenepo Mose analandira ndalama zoombola nazo kwa iwo akuposa aja adawaombola Alevi;

50 analandira ndalamazo kwa oyamba kubadwa a ana a Israele; masekeli chikwi chimodzi mphambu mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi mphambu asanu, kuyesa sekeli wa malo opatulika.

51 Ndipo Mose anapatsa Aroni ndi ana ake ndalama zoombola nazo monga mwa mau a Yehova, monga Yehova adauza Mose.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/3-8c7569445f97a1370a6179678964d489.mp3?version_id=1068—

Categories
NUMERI

NUMERI 4

Akohati

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

2 Werengani ana a Kohati pakati pa ana a Levi, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao,

3 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu, kufikira zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kuti agwire ntchito yachihema chokomanako.

4 Ntchito ya ana a Kohati m’chihema chokomanako ndi iyi, kunena za zinthu zopatulika kwambiri:

5 akati amuke a m’chigono, Aroni ndi ana ake aamuna azilowa, natsitse nsalu yotchinga, ndi kuphimba nayo likasa la mboni,

6 ndi kuikapo chophimba cha zikopa za akatumbu; ndi kuyalapo nsalu yamadzi yeniyeni, ndi kupisako mphiko zake.

7 Ndi pa gome la mkate woonekera ayale nsalu yamadzi, naikepo mbale zake, ndi zipande, ndi mitsuko, ndi zikho zakuthira nazo; mkate wa chikhalire uzikhalaponso.

8 Ndipo ayale pa izi nsalu yofiira, ndi kuliphimba ndi chophimba cha zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zake.

9 Ndipo atenge nsalu yamadzi, ndi kuphimba choikaponyali younikira, ndi nyali zake, ndi mbano zake, ndi zoolera zake, ndi zotengera zake zonse za mafuta zogwira nazo ntchito yake.

10 Ndipo achimange ndi chipangizo zake zonse m’chophimba cha zikopa za akatumbu, ndi kuziika pa chonyamulira.

11 Ndipo paguwa la nsembe lagolide aziyala nsalu ya madzi, naliphimbe ndi chophimba cha zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zake.

12 Natenge zipangizo zake zonse za utumiki, zimene atumikira nazo m’malo opatulika, nazimange m’nsalu yamadzi, ndi kuziphimba ndi chophimba cha zikopa za akatumbu, ndi kuziika pachonyamulira.

13 Ndipo azichotsa mapulusa paguwa la nsembe, ndi kuyala pa ilo nsalu yofiirira.

14 Naikepo zipangizo zake zonse, zimene atumikira nazo pamenepo, mbale za zofukiza, mitungo, ndi zoolera, ndi mbale zowazira, zipangizo zonse za guwa la nsembe; nayalepo chophimba cha zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zake.

15 Atatha Aroni ndi ana ake aamuna kuphimba malo opatulika, ndi zipangizo zake zonse za malo opatulika, pofuna kumuka am’chigono; atatero, ana a Kohati adze kuzinyamula; koma asakhudze zopatulikazo, kuti angafe. Zinthu izi ndizo akatundu a ana a Kohati m’chihema chokomanako.

16 Ndipo zoyang’anira Eleazara, mwana wa Aroni wansembe, ndizo mafuta a nyaliyo, ndi chofukiza cha fungo lokoma, ndi nsembe yaufa kosalekeza, ndi mafuta odzoza, udikiro wa chihema chonse, ndi zonse zili m’mwemo, malo opatulika, ndi zipangizo zake.

17 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

18 Musamasadza fuko la mabanja a Akohati kuwachotsa pakati pa Alevi;

19 koma muzitero nao kuti akhale ndi moyo, osafa ai, poyandikiza iwo zopatulika kwambirizo; Aroni ndi ana ake aamuna alowe, namuikire munthu yense ntchito yake ndi katundu wake.

20 Koma asalowe kukaona zopatulikazo pozikulunga, kuti angafe.

Ageresoni

21 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

22 Werenganso ana a Geresoni, monga mwa nyumba za makolo ao, monga mwa mabanja ao.

23 Uwawerenge kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu, kufikira a zaka makumi asanu; onse akulowa kutumikira utumikiwo, kuchita ntchitoyi m’chihema chokomanako.

24 Ntchito ya mabanja a Ageresoni, pogwira ntchito ndi kusenza katundu ndi iyi;

25 azinyamula nsalu zophimba za Kachisi, ndi chihema chokomanako, chophimba chake, ndi chophimba cha zikopa za akatumbu chili pamwamba pake, ndi nsalu yotsekera pa khomo la chihema chokomanako;

26 ndi nsalu zotchingira za pabwalo, ndi nsalu yotsekera ku chipata cha pabwalo lili pa chihema ndi paguwa la nsembe pozungulira, ndi zingwe zao, ndi zipangizo zonse za ntchito zao, ndi zonse achita nazo; m’menemo muli ntchito zao.

27 Ntchito yonse ya ana a Ageresoni, kunena za akatundu ao ndi ntchito zao zonse, ikhale monga adzanena Aroni ndi ana ake aamuna; ndipo muwaike adikire akatundu ao onse.

28 Iyi ndi ntchito ya mabanja a ana a Geresoni m’chihema chokomanako; ndipo Itamara mwana wa Aroni wansembe ayang’anire udikiro wao.

Amerari

29 Kunena za ana a Merari, Uwawerenge monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao.

30 Uwawerenge kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kuchita ntchito ya chihema chokomanako.

31 Ndipo udikiro wa akatundu ao, monga mwa ntchito zao zonse m’chihema chokomanako ndi ichi: matabwa a Kachisi, ndi mitanda yake, ndi mizati ndi nsanamira zake, ndi makamwa ake;

32 ndi nsichi za kubwalo kozungulira, ndi makamwa ake, ndi zichiri zake, ndi zingwe zake, pamodzi ndi zipangizo zake zonse, ndi ntchito yake yonse; ndipo muziwerenga zipangizo za udikiro wa akatundu ao ndi kuwatchula maina ao.

33 Iyi ndi ntchito ya mabanja a ana a Merari, monga mwa ntchito zao zonse m’chihema chokomanako, mowauza Itamara mwana wa Aroni wansembe.

34 Ndipo Mose ndi Aroni ndi akalonga a khamu anawerenga ana a Akohati monga mwa mabanja ao, ndi monga mwa nyumba za makolo ao,

35 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kuti agwire ntchito m’chihema chokomanako;

36 ndipo owerengedwa ao monga mwa mabanja ao ndiwo zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu.

37 Awa ndi owerengedwa a mabanja a Akohati, onse akutumikira m’chihema chokomanako, amene Mose ndi Aroni anawawerenga monga mwa mau a Yehova mwa dzanja la Mose.

38 Ndipo ana owerengedwa a Geresoni, monga mwa mabanja ao, ndi monga mwa nyumba za makolo ao,

39 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kuti agwire ntchito m’chihema chokomanako,

40 owerengedwa ao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, ndiwo zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi limodzi kudza makumi atatu.

41 Amenewo ndiwo owerengedwa a mabanja a ana a Geresoni, onse akutumikira m’chihema chokomanako, adawawerenga Mose ndi Aroni monga mwa mau a Yehova.

42 Ndipo owerengedwa a mabanja a ana a Merari, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao,

43 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu kuti agwire ntchito m’chihema chokomanako,

44 owerengedwa ao monga mwa mabanja ao, ndiwo zikwi zitatu ndi mazana awiri.

45 Amenewo ndiwo owerengedwa a mabanja a ana a Merari, amene Mose ndi Aroni anawawerenga monga mwa mau a Yehova mwa dzanja la Mose.

Kuwerengedwa kwa Alevi

46 Owerengedwa onse a Alevi, amene Mose ndi Aroni ndi akalonga a Israele anawawerengera, monga mwa mabanja ao, ndi monga mwa nyumba za makolo ao,

47 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa kugwira ntchito ya utumikiwu, ndiyo ntchito ya akatundu m’chihema chokomanako;

48 owerengedwawo ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu kudza mazana asanu mphambu makumi asanu ndi atatu.

49 Anawawerenga monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose, onse monga mwa ntchito zao, ndi monga mwa akatundu ao; anawawerenga monga momwe Yehova adauza Mose.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/4-69210a7770783054ae8af162d34f1725.mp3?version_id=1068—

Categories
NUMERI

NUMERI 5

Odetsedwa onse achotsedwe kuchigono

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2 Uza ana a Israele kuti azitulutsa m’chigono akhateonse, ndi onse akukhala nako kukha, ndi onse odetsedwa chifukwa cha akufa;

3 muwatulutse amuna ndi akazi muwatulutsire kunja kwa chigono, kuti angadetse chigono chao, chimene ndikhala m’kati mwakemo.

4 Ndipo ana a Israele anachita chotero, nawatulutsira kunja kwa chigono; monga Yehova adanena ndi Mose momwemo ana a Israele anachita.

Za kubwezera

5 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

6 Nena ndi ana a Israele, ndi kuti Mwamuna kapena mkazi akachita tchimo lililonse amachita anthu, kuchita mosakhulupirika pa Yehova, nakapalamuladi;

7 azivomereza tchimo lake adalichita; nabwezere chopalamulacho monsemo, naonjezeko limodzi la magawo asanu, ndi kuchipereka kwa iye adampalamulayo.

8 Koma munthuyo akapanda kukhala nayo nkhoswe imene akaibwezere chopalamulacho, chopalamula achibwezera Yehovacho chikhale cha wansembe; pamodzi ndi nkhosa yamphongo ya chotetezerapo, imene amchitire nayo chomtetezera.

9 Ndipo nsembe zokweza zonse za zinthu zopatulika za ana a Israele, zimene abwera nazo kwa wansembe zisanduka zake.

10 Zopatulika za munthu aliyense ndi zake: zilizonse munthu aliyense akapatsa wansembe, zisanduka zake.

Za mlandu wa nsanje

11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

12 Nena ndi ana a Israele, nuti nao, Mkazi wamwini akapatukira mwamuna wake, nakamchitira mosakhulupirika,

13 ndi munthu akagona naye, koma kumbisikira maso a mwamuna wake, ndi kumng’unira; nadetsedwa mkaziyo, koma palibe mboni yomtsutsa, kapena sanamgwire alimkuchita;

14 ndipo ukamgwira mwamuna mtima wansanje, kuti achitire nsanje mkazi wake, popeza wadetsedwa; kapena ukamgwira mtima wansanje, kuti amchitire mkazi wake nsanje angakhale sanadetsedwe;

15 pamenepo mwamunayo azidza naye mkazi wake kwa wansembe, nadze nacho chopereka chake, limodzi la magawo khumi la efa wa ufa wabarele; asathirepo mafuta, kapena kuikapolubani; popeza ndiyo nsembe yaufa yansanje, nsembe yaufa yachikumbutso, yakukumbutsa mphulupulu.

16 Ndipo wansembe abwere naye, namuike pamaso pa Yehova;

17 natenge madzi opatulika m’mbale yadothi wansembeyo, natengeko fumbi lili pansi mu chihema, wansembeyo nalithire m’madzimo.

18 Pamenepo wansembeyo aike mkaziyo pamaso pa Yehova, navula mutu wa mkaziyo, naike nsembe yaufa yachikumbutso m’manja mwake, ndiyo nsembe yaufa yansanje; ndipo m’manja mwake mwa wansembe muzikhala madzi owawa akudzetsa temberero.

19 Ndipo wansembe amlumbiritse, nanene kwa mkazi, Ngati sanagone nawe munthu mmodzi yense, ngati sunapatukire kuchidetso, pokhala ndiwe wa mwamuna wako, upulumuke ku madzi owawa awa akudzetsa temberero.

20 Koma iwe, ngati wapatukira mwamuna wako, ngati wadetsedwa, kuti wagona nawe munthu, wosati mwamuna wako;

21 pamenepo wansembe alumbiritse mkazi lumbiro lakutemberera, ndi wansembe anene kwa mkazi, Yehova akuike ukhale temberero ndi lumbiro pakati pa anthu a mtundu wako, pakuondetsa Yehova m’chuuno mwako, ndi kukutupitsa thupi lako;

22 ndipo madzi awa akudzetsa temberero adzalowa m’matumbo mwako, nadzakutupitsa thupi lako ndi kuondetsa m’chuuno mwako; ndipo mkaziyo aziti,Amen, Amen.

23 Ndipo wansembe alembere matemberero awa m’buku, ndi kuwafafaniza ndi madzi owawawa.

24 Ndipo amwetse mkaziyo madzi owawa akudzetsa temberero; ndi madzi odzetsa temberero adzalowa mwa iye nadzamwawira.

25 Ndipo wansembe atenge nsembe yaufa yansanje m’manja mwa mkazi, naweyule nsembe yaufa pamaso pa Yehova, nabwere nayo ku guwa la nsembe.

26 Wansembe atengekonso nsembe yaufa wodzala manja, chikumbutso chake, nachitenthe paguwa la nsembe; ndipo atatero amwetse mkazi madziwo.

27 Ndipo atammwetsa madziwo, kudzatero, ngati wadetsedwa, nachita mosakhulupirika pa mwamuna wake, madzi odzetsa tembererowo adzalowa mwa iye nadzamwawira, nadzamtupitsa thupi lake, ndi m’chuuno mwake mudzaonda; ndi mkaziyo adzakhala temberero pakati pa anthu a mtundu wake.

28 Koma ngati mkazi sanadetsedwe, nakhala woyera, pamenepo adzapulumuka, nadzaima.

29 Ichi ndi chilamulo cha nsanje, pamene mkazi, pokhala naye mwamuna wake, ampatukira nadetsedwa;

30 kapena pamene mtima wansanje umgwira mwamuna, ndipo achitira mkazi wake nsanje; pamenepo aziika mkazi pamaso pa Yehova, ndipo wansembe amchitire chilamulo ichi chonse.

31 Mwamunayo ndiye wosachita mphulupulu, koma mkazi uyo asenze mphulupulu yake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/5-f345073e9dc6f00e3f6b266273bf68e4.mp3?version_id=1068—

Categories
NUMERI

NUMERI 6

Za chowinda cha Mnaziri

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Nena ndi ana a Israele, nuti nao, Mwamuna kapena mkazi akadzipatulira kulonjeza chowinda chaMnaziri, kudzipatulira kwa Yehova;

3 azisala vinyo ndi kachasu; asamwe vinyo wosasa, kapena kachasu wosasa, kapena chakumwa chonse cha mphesa, asamwe; asadye mphesa zaziwisi kapena zouma.

4 Masiku onse a kusala kwake asadye kanthu kopangika ndi mphesa, kuyambira nthanga zake kufikira khungu lake.

5 Masiku onse a chowinda chake chakusala, lumo lisapite pamutu pake; kufikira adatha masikuwo adadzipatulira kwa Yehova, azikhala wopatulika; aleke nzera za tsitsi lake zimeretu.

6 Masiku onse akudzipatulira kwa Yehova asayandikize mtembo.

7 Asadzidetse ndi atate wake, kapena mai wake, mbale wake, kapena mlongo wake, akafa iwowa; popeza chowindira Mulungu wake chili pamutu pake.

8 Masiku onse a kusala kwake akhala wopatulikira kwa Yehova.

9 Munthu akafa chikomo pali iye, ndipo akadetsa mutu wake wowinda; pamenepo azimeta mutu wake tsiku la kumyeretsa kwake, tsiku lachisanu ndi chiwiri aumete.

10 Ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu adze nazo njiwa ziwiri, kapena maunda awiri, kwa wansembe; ku khomo lachihema chokomanako;

11 ndipo wansembe akonze imodzi nsembe yauchimo, ndi ina nsembe yopsereza, namtetezere popeza anachimwa nao mtembowo; ndipo apatulire mutu wake tsiku lomwelo.

12 Ndipo awapatulire Yehova masiku a kusala kwake, nadze nayo nkhosa yamphongo ya chaka chimodzi ikhale nsembe yopalamula; koma masiku adapitawa azikhala chabe, popeza anadetsa kusala kwake.

13 Ndipo chilamulo cha Mnaziri, atatha masiku a kusala kwake ndi ichi: azidza naye ku khomo la chihema chokomanako;

14 pamenepo abwere nacho chopereka chake kwa Yehova, nkhosa yamphongo ya chaka chimodzi yopanda chilema, ikhale nsembe yopsereza, ndi nkhosa yaikazi yopanda chilema ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa yamphongo yopanda chilema ikhale nsembe yoyamika;

15 ndi dengu la mkate wopanda chotupitsa, timitanda ta ufa wosalala tosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda taphanthi todzoza ndi mafuta, ndi nsembe yao yaufa, ndi nsembe zao zothira.

16 Ndipo wansembe azibwera nazo pamaso pa Yehova, nakonze nsembe yake yauchimo, ndi nsembe yake yopsereza;

17 naphe nkhosa yamphongo yoyamika ya Yehova, pamodzi ndi dengu la mkate wopanda chotupitsa; wansembe akonzenso nsembe yake yaufa, ndi nsembe yake yothira.

18 Pamenepo Mnaziriyo amete mutu wake wa kusala kwake pa khomo la chihema chokomanako, natenge tsitsi la pamutu wake wa kusala, naliike pamoto wokhala pansi pa nsembe yoyamika.

19 Ndipo wansembe atenge mwendo wammwamba wophika wa nkhosa yamphongo, ndi kamtanda kamodzi kopanda chotupitsa ka m’dengu, ndi kamtanda kaphanthi kopanda chotupitsa kamodzi, ndi kuziika m’manja mwa Mnaziri, atameta kusala kwake;

20 ndipo wansembe aziweyula nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ichi nchopatulikira wansembe, pamodzi ndi nganga ya nsembe yoweyula, pamodzi ndi mwendo wa nsembe yokweza; ndipo atatero Mnaziri amwe vinyo.

21 Ichi ndi chilamulo cha Mnaziri wakuwinda, ndi cha chopereka chake cha Yehova chifukwa cha kusala kwake, pamodzi nacho chimene dzanja lake likachipeza; azichita monga mwa chowinda chake anachiwinda, mwa chilamulo cha kusala.

Mau a mdalitso

22 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

23 Nena ndi Aroni ndi ana ake, ndi kuti, Uzidalitsa ana a Israele motero; uziti nao,

24 Yehova akudalitse iwe, nakusunge;

25 Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitire chisomo;

26 Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.

27 Potero aike dzina langa pa ana a Israele; ndipo ndidzawadalitsa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/6-2401033b2d76e94e89ddda1d669e4bfb.mp3?version_id=1068—

Categories
NUMERI

NUMERI 7

Zopereka za Akulu 12 atautsa chihemacho

1 Ndipo kunali kuti tsiku lomwe Mose anatsiriza kuutsa chihema, nachidzoza ndi kuchipatula, ndi zipangizo zake zonse, ndi guwa la nsembe, ndi zipangizo zake zonse, nazidzoza ndi kuzipatula;

2 akalonga a Israele, akulu a nyumba za makolo ao, anapereka nsembe, ndiwo akalonga a mafuko akuyang’anira owerengedwa;

3 anadza nacho chopereka chao pamaso pa Yehova, magaleta ophimbika asanu ndi mmodzi, ndi kalonga awiru anapereka galeta ndi kalonga mmodzi ng’ombe imodzi; nabwera nazo pakhomo pa chihema.

4 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

5 Uzilandira kwa iwo, kuti zikhale zakuchitira ntchito yachihema chokomanako; nuzipereke kwa Alevi, yense monga mwa ntchito yake.

6 Ndipo Mose analandira magaleta ndi ng’ombe, nazipereka kwa Alevi.

7 Anapatsa ana a Geresoni magaleta awiri ndi ng’ombe zinai, monga mwa ntchito yao;

8 napatsa ana a Merari magaleta anai ndi ng’ombe zisanu ndi zitatu, monga mwa ntchito yao; wakuziyang’anira ndiye Itamara mwana wa Aroni wansembe.

9 Koma sanapatse ana a Kohati kanthu; popeza ntchito yao ndiyo ya zinthu zopatulika, zimene amazisenza pa mapewa ao.

10 Ndipo akalonga anabwera nazo za kupereka chiperekere guwa la nsembe tsiku lodzozedwa ili; inde akalongawo anabwera nacho chopereka chao paguwa la nsembelo.

11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Akalonga onse, yense pa tsiku lake, apereke zopereka zao za kupereka chiperekere guwa la nsembe.

12 Wakubwera nacho chopereka chake tsiku loyamba ndiye Nasoni mwana wa Aminadabu, wa fuko la Yuda:

13 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake ndiko masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwirizo zodzala ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ukhale nsembe yaufa;

14 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

15 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi,mwanawankhosammodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

16 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

17 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Nasoni mwana wa Aminadabu.

18 Tsiku lachiwiri Netanele mwana wa Zuwara, kalonga wa Isakara, anabwera nacho chake:

19 anabwera nacho chopereka chake mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

20 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

21 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

22 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

23 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Netanele mwana wa Zuwara.

24 Tsiku lachitatu kalonga wa ana a Zebuloni, ndiye Eliyabu mwana wa Heloni:

25 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzaza ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

26 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

27 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

28 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

29 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Eliyabu mwana wa Heloni.

30 Tsiku lachinai Elizuri, mwana wa Sedeuri, kalonga wa ana a Rubeni:

31 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika, zonse ziwiri zodzaza ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

32 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

33 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

34 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

35 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.

36 Tsiku lachisanu kalonga wa ana a Simeoni, ndiye Selumiele, mwana wa Zurishadai:

37 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

38 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

39 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

40 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

41 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Selumiele mwana wa Zurishadai.

42 Tsiku lachisanu ndi chimodzi kalonga wa ana a Gadi, Eliyasafu mwana wa Deuwele:

43 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu; mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

44 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

45 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

46 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

47 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuwele.

48 Tsiku lachisanu ndi chiwiri kalonga wa ana a Efuremu Elisama mwana wa Amihudi:

49 chopereka chake mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

50 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

51 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

52 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

53 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa za mphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.

54 Tsiku lachisanu ndi chitatu kalonga wa ana a Manase ndiye Gamaliele mwana wa Pedazuri:

55 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

56 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

57 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

58 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

59 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Gamaliele mwana wa Pedazuri.

60 Tsiku lachisanu ndi chinai kalonga wa ana a Benjamini, ndiye Abidani mwana wa Gideoni:

61 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

62 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

63 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

64 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

65 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.

66 Tsiku lakhumi kalonga wa ana a Dani, ndiye Ahiyezere mwana wa Amisadai:

67 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosakaniza ndi mafuta ukhale nsembe yaufa;

68 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

69 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

70 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

71 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Ahiyezere mwana wa Amisadai.

72 Tsiku la khumi ndi limodzi kalonga wa ana a Asere, ndiye Pagiyele mwana wa Okarani;

73 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

74 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

75 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

76 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

77 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ndicho chopereka cha Pagiyele mwana wa Okarani.

78 Tsiku lakhumi ndi chiwiri kalonga wa ana a Nafutali, ndiye Ahira mwana wa Enani:

79 chopereka chake ndicho mbale imodzi yasiliva, kulemera kwake masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosakaniza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

80 chipande chimodzi chagolide cha masekeli khumi, chodzala ndi chofukiza;

81 ng’ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwanawankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

82 tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo;

83 ndi nsembe yoyamika, ng’ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, anaankhosa asanu a chaka chimodzi; ichi ndi chopereka cha Ahira mwana wa Enani.

84 Uku ndi kupereka chiperekere guwa la nsembe, ndi akalonga a Israele, tsiku la kudzoza kwake: mbale zasiliva khumi ndi ziwiri, mbale zowazira zasiliva khumi ndi ziwiri, zipande zagolide khumi ndi ziwiri;

85 mbale yasiliva yonse masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, ndi mbale yowazira yonse masekeli makumi asanu ndi awiri; siliva wonse wa zotengerazo ndizo masekeli zikwi ziwiri ndi mazana anai, kuyesa sekeli wa malo opatulika.

86 Zipande zagolide ndizo khumi ndi ziwiri, zodzala ndi chofukiza, chipande chonse masekeli khumi, kuyesa sekeli wa malo opatulika; golide wonse wa zipandezo ndiwo masekeli zana limodzi ndi makumi awiri;

87 ng’ombe zonse za nsembe yopsereza ndizo ng’ombe khumi ndi ziwiri, nkhosa zamphongo khumi ndi ziwiri, anaankhosa a chaka chimodzi khumi ndi awiri, pamodzi ndi nsembe yao yaufa; ndi atonde a nsembe zauchimo khumi ndi awiri;

88 ndi ng’ombe zonse za nsembe yoyamika ndizo ng’ombe makumi awiri ndi zinai, nkhosa zamphongo makumi asanu ndi limodzi, atonde makumi asanu ndi limodzi, anaankhosa a chaka chimodzi makumi asanu ndi limodzi. Uku ndi kupereka chiperekere, litadzozedwa guwa la nsembe.

89 Ndipo polowa Mose ku chihema chokomanako, kunena ndi Iye, anamva mau akunena naye ochokera ku chotetezerapo chili pa likasa la mboni, ochokera pakati paakerubiawiriwo; ndipo Iye ananena naye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/7-72e329c1fb0c6c10869cbe6d634d0c18.mp3?version_id=1068—

Categories
NUMERI

NUMERI 8

Za kuyatsa nyalizo

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Nena kwa Aroni, nuti naye, Pamene uyatsa nyalizo, nyali zisanu ndi ziwirizo ziwale pandunji pake pa choikaponyalicho.

3 Ndipo Aroni anachita chotero; anayatsa nyalizo kuti ziwale pandunji pake pa choikaponyali, monga Yehova adauza Mose.

4 Ndipo mapangidwe ake a choikaponyali ndiwo golide wosula; kuyambira tsinde lake kufikira maluwa ake anachisula; monga mwa maonekedwe ake Yehova anaonetsa Mose, momwemo anachipanga choikaponyali.

Za kuyeretsa Alevi

5 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

6 Uwatenge Alevi pakati pa ana a Israele, nuwayeretse.

7 Ndipo utere nao kuwayeretsa: uwawaze madzi akuchotsa zoipa, ndipo apititse lumo pa thupi lao lonse, natsuke zovala zao, nadziyeretse.

8 Pamenepo atenge ng’ombe yamphongo ndi nsembe yake yaufa, ufa wosakaniza ndi mafuta; utengenso ng’ombe yamphongo ina ikhale nsembe yauchimo.

9 Ndipo ubwere nao Alevi pakhomo pachihema chokomanako; nuwasonkhanitse khamu lonse la ana a Israele;

10 nubwere nao Alevi pamaso pa Yehova; ndi ana a Israele aike manja ao pa Alevi;

11 ndi Aroni apereke Alevi ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova, yochokera kwa ana a Israele, kuti akhale akuchita ntchito ya Yehova.

12 Ndipo Alevi aike manja ao pa mitu ya ng’ombezo; pamenepo ukonze imodzi ikhale nsembe yauchimo, ndi inzake, nsembe yopsereza za Yehova, kuchita chotetezera Alevi.

13 Ndipo uimike Alevi pamaso pa Aroni, ndi pamaso pa ana ake, ndi kuwapereka ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.

14 Momwemo upatule Alevi mwa ana a Israele; kuti Alevi akhale anga.

15 Ndipo atatero alowe Alevi kuchita ntchito ya chihema chokomanako; ndipo uwayeretse, ndi kuwapereka ngati nsembe yoweyula.

16 Pakuti aperekedwa konse kwa Ine ochokera mwa ana a Israele; ndadzitengera iwo m’malo mwa onse akutsegula mimba, ndiwo oyamba kubadwa a ana a Israele.

17 Pakuti oyamba kubadwa onse mwa ana a Israele ndi anga, mwa anthu ndi zoweta; tsiku lija ndinakantha oyamba kubadwa onse m’dziko la Ejipito, ndinadzipatulira iwo akhale anga.

18 Ndipo ndatenga Alevi m’malo mwa oyamba kubadwa onse mwa ana a Israele.

19 Ndipo ndapereka Alevi akhale mphatso ya kwa Aroni ndi ana ake aamuna yochokera mwa ana a Israele, kuchita ntchito ya ana a Israele, m’chihema chokomanako ndi kuchita chotetezera ana a Israele; kuti pasakhale mliri pakati pa ana a Israele, pakuyandikiza ana a Israele ku malo opatulika.

20 Ndipo Mose ndi Aroni ndi khamu lonse la ana a Israele anachitira Alevi monga mwa zonse Yehova adauza Mose kunena za Alevi; momwemo ana a Israele anawachitira.

21 Ndipo Alevi anadziyeretsa, natsuka zovala zao; ndi Aroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ndi Aroni anawachitira chotetezera kuwayeretsa.

22 Ndipo atatero, Alevi analowa kuchita ntchito yao m’chihema chokomanako pamaso pa Aroni, ndi pamaso pa ana ake aamuna; monga Yehova analamula Mose kunena za Alevi, momwemo anawachitira.

23 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

24 Ichi ndi cha Alevi: kuyambira ali wa zaka makumi awiri ndi zisanu ndi mphambu azilowa kutumikira utumikiwu mu ntchito ya chihema chokomanako;

25 ndipo kuyambira zaka makumi asanu azileka kutumikira utumikiwu, osachitanso ntchitoyi;

26 koma atumikire pamodzi ndi abale ao m’chihema chokomanako, kusunga udikirowo, koma osagwira ntchito. Utere nao Alevi kunena za udikiro wao.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/8-88134c05685c8afa3502c32b29e93334.mp3?version_id=1068—

Categories
NUMERI

NUMERI 9

Achita Paska

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m’chipululu cha Sinai, mwezi woyamba wa chaka chachiwiri atatuluka m’dziko la Ejipito, ndi kuti,

2 Ana a Israele achitePaskapa nyengo yoikidwa.

3 Tsiku lakhumi ndi chinai la mweziwo, madzulo, muziuchita, pa nyengo yake yoikidwa; muuchite monga mwa malemba ake onse, ndi maweruzo ake onse.

4 Ndipo Mose ananena ndi ana a Israele, kuti achite Paska.

5 Ndipo anachita Paska mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi chinai la mweziwo, madzulo m’chipululu cha Sinai; monga mwa zonse Yehova adauza Mose, momwemo ana a Israele anachita.

6 Pamenepo panali amuna, anadetsedwa ndi mtembo wa munthu, ndipo sanakhoze kuchita Paska tsiku lomwelo; m’mwemo anafika pamaso pa Mose ndi pamaso pa Aroni tsiku lomwelo;

7 nanena naye amunawa, Tadetsedwa ife ndi mtembo wa munthu; atiletseranji, kuti tisabwere nacho chopereka cha Yehova pa nyengo yake yoikidwa, pakati pa ana a Israele?

8 Ndipo Mose ananena nao, Baimani; ndimve chouza Yehova za inu.

9 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

10 Nena ndi ana a Israele, ndi kuti, Angakhale munthu wa inu kapena wa mibadwo yanu, adetsedwa, chifukwa cha mtembo, kapena pokhala paulendo, koma azichitira Yehova Paska.

11 Mwezi wachiwiri, tsiku lake lakhumi ndi chinai, madzulo, auchite; audye ndi mkate wopanda chotupitsa ndi msuzi wowawa.

12 Asasiyeko kufikira m’mawa, kapena kuthyolapo fupa; auchite monga mwa lemba lonse la Paska.

13 Munthu akakhala woyera, wosakhala paulendo, koma akaleka kuchita Paska, amsadze munthuyo kwa anthu a mtundu wake; popeza sanabwere nacho chopereka cha Yehova pa nyengo yake yoikidwa, munthuyu asenze kuchimwa kwake.

14 Ndipo mlendo akakhala mwa inu, nakachitira Yehova Paska, azichita monga mwa lemba la Paska, ndi monga mwa chiweruzo chake; lemba likhale limodzi kwa inu, ndi kwa mlendo, ndi kwa wobadwa m’dziko.

Mtambo pamwamba pa Kachisi

15 Ndipo tsiku loutsa Kachisi mtambo unaphimba Kachisi, ndiwochihema chokomanako; ndicho chihema chaumboni, ndipo madzulo padaoneka pa Kachisi ngati moto, kufikira m’mawa.

16 Kudatero kosalekeza; mtambo umachiphimba, ndi moto umaoneka usiku.

17 Ndipo pokwera mtambo kuchokera kuchihema, utatero ana a Israele amayenda ulendo wao; ndipo pamalo pokhala mtambo, pamenepo ana a Israele amamanga mahema ao.

18 Pakuwauza Yehova ana a Israele amayenda ulendo, powauza Yehova amamanga mahema ao; masiku onse mtambo ukakhala pamwamba pa chihema amakhala m’chigono.

19 Ndipo pakukhalitsa mtambo masiku ambiri pamwamba pa chihema, pamenepo ana a Israele anasunga udikiro wa Yehova osayenda ulendo.

20 Ndipo pokhala mtambo pamwamba pa chihema masiku pang’ono; pamenepo anakhala m’chigono monga awauza Yehova, nayendanso ulendo monga anauza Yehova.

21 Koma mtambo ukakhala kuyambira madzulo kufikira m’mawa; pokwera mtambo m’mawa, ayenda ulendo.

22 Ngakhale masiku awiri, kapena mwezi, kapena masiku ambiri, pokhalitsa mtambo pamwamba pa chihema ndi kukhalapo, ana a Israele anakhala m’chigono, osayenda ulendo; koma pakukwera uwu, anayenda ulendo.

23 Powauza Yehova amanga mahema, powauza Yehova ayenda ulendo; anasunga udikiro wa Yehova powauza Yehova mwa dzanja la Mose.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/9-7401ea656470e41cd4b00b8b6ed75cc5.mp3?version_id=1068—