Categories
MLALIKI

MLALIKI 10

Kupusa kusautsa kwambiri

1 Ntchentche zakufa zinunkhitsa moipa ndipo zioletsa mafuta onunkhira a sing’anga; chomwecho kupusa kwapang’ono kuipitsa iye amene atchuka chifukwa cha nzeru ndi ulemu.

2 Wanzeru, mtima wake uli kudzanja lake lamanja; koma chitsiru, mtima wake kulamanzere.

3 Inde, poyendanso chitsiru panjira, nzeru yake imthera ndipo angoti kwa onse kuti, Ndine chitsiru.

4 Ngati mkulu akukwiyira, usasiye malo ako; chifukwa chifatso chipembedza utachimwa kwambiri.

5 Pali choipa ndachiona pansi pano, ngati kulakwa koyambira ndi mkulu;

6 utsiru ukhazikika pamwamba penipeni, ndipo olemera angokhala mwamanyazi.

7 Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, ndi mafumu, alikuyenda pansi ngati akapolo.

8 Wokumba mbuna adzagwamo; ndipo woboola mpanda njoka idzamluma.

9 Wosendeza miyala adzaphwetekedwa nayo; wowaza nkhuni nadzitema.

10 Chitsulo chikakhala chosathwa, ndipo ukaleka kunola, uzipambana kulimbikira; koma nzeru ipindulira pochenjeza.

11 Njoka ikaluma isanalodzedwe, watsenga saona mphotho.

12 Mau a m’kamwa mwa munthu wanzeru nga chisomo; koma milomo ya chitsiru idzachimeza.

13 Chiyambi cha mau a m’kamwa mwake ndi utsiru; ndipo chimaliziro cha m’kamwa mwake ndi misala yoipa.

14 Chitsiru chichulukitsanso mau; koma munthu sadziwa chimene chidzaoneka; ndipo ndani angamuuze chomwe chidzakhala m’tsogolo mwake?

15 Ntchito ya zitsiru izitopetsa zonsezo, pakuti sichidziwa kunka kumzinda.

16 Tsoka kwa dzikowe, pamene mfumu yako ndiye mwana, ndipo akalonga ako adyera mamawa!

17 Mwai kwa dzikowe, pamene mfumu yako ndiye mwana wa aufulu, ndipo akalonga ako adya pa nthawi yoyenera akalimbe osati akaledzere ai.

18 Tsindwi litewa ndi mphwai za eni ake; nyumba nidontha ndi ulesi wa manja.

19 Amaphikira zakudya kuti asekere, vinyo nakondweretsa moyo; ndipo ndalama zivomera zonse.

20 Usatemberere mfumu ngakhale poganizira; usatemberere wolemera m’chipinda chogona iwemo; pakuti mbalame ya mlengalenga idzanyamula mauwo, ndipo chouluka ndi mapiko chidzamveketsa zonenazo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ECC/10-c5997c02314d8b076605291309817397.mp3?version_id=1068—

Categories
MLALIKI

MLALIKI 11

Tizichita zokoma lero lino posadziwa za mawa

1 Ponya zakudya zako pamadzi; udzazipeza popita masiku ambiri.

2 Gawira asanu ndi awiri ngakhale asanu ndi atatu; pakuti sudziwa choipa chanji chidzaoneka pansi pano.

3 Mitambo ikadzala mvula, itsanulira pansi; mtengo ukagwa kumwera pena kumpoto, pomwe unagwa mtengowo udzakhala pomwepo.

4 Woyang’ana mphepo sadzafesa; ndi wopenya mitambo sadzakolola.

5 Monga sudziwa njira ya mphepo, ngakhale makulidwe a mafupa m’mimba ya mkazi ali ndi pakati; momwemo sudziwa ntchito za Mulungu amene achita zonse.

6 Mamawa fesa mbeu zako, madzulonso osapumitsa dzanja lako; pakuti sudziwa ziti zidzalola bwino ngakhale izizi, ngakhale izozo, kaya zonse ziwiri zidzakhala bwino.

7 Indetu kuunika nkokoma, maso napeza bwino m’kuona dzuwa.

8 Inde, munthu akakhala ndi moyo zaka zambiri, akondwere ndi zonsezo; koma akumbukire masiku amdima kuti adzachuluka. Zonse zilinkudza zili zachabe.

Anyamata asangalale, koma adzikonzeretu pokumbukira imfa ikudza

9 Kondwera ndi unyamata wako, mnyamata iwe; mtima wako nukasangalale masiku a unyamata wako, nuyende m’njira za mtima wako, ndi monga maso ako aona; koma dziwitsa kuti Mulungu adzanena nawe mlandu wa zonsezi.

10 Chifukwa chake chotsani zopweteka m’mtima mwako, nulekanitse zoipa ndi thupi lako; pakuti ubwana ndi unyamata ngwa chabe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ECC/11-490240226c1c1418d83865f9ce75f2a3.mp3?version_id=1068—

Categories
MLALIKI

MLALIKI 12

1 Ukumbukirenso Mlengi wako masiku a unyamata wako, asanadze masiku oipa, ngakhale zisanayandikire zakazo zakuti udzati, Sindikondwera nazo;

2 ngakhale lisanade dzuwa, ndi kuunika, ndi mwezi, ndi nyenyezi, mitambo ndi kubweranso italeka mvula;

3 tsikulo omwe asunga nyumba adzanthunthumira, amuna olimba nadzawerama, akupera nadzaleka poperewera, omwe ayang’ana pamazenera nadzadetsedwa;

4 pa khomo lakunja padzatsekeka; potsika mau akupera, wina nanyamuka polira mbalame, ndipo akazi onse akuimba sadzamveka bwino;

5 inde, adzaopa za pamwamba, panjira padzakhala zoopsa; katungurume adzaphuka, dzombe ndi kukoka miyendo, zilakolako ndi kutha; pakuti munthu apita kwao kwamuyaya, akulira maliro nayendayenda panja;

6 chingwe chasilivachisanaduke, ngakhale mbale yagolide isanasweke, ngakhale mtsuko usanaphwanyike kukasupe, ngakhale njinga yotungira madzi isanathyoke kuchitsime;

7 fumbi ndi kubwera pansi pomwe linali kale, mzimu ndi kubwera kwa Mulungu amene anaupereka.

8 Chabe zachabetu, ati Mlalikiyo; zonse ndi chabe.

Zoyenera munthu ndizo kuopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake

9 Ndiponso pokhala wanzeru Mlalikiyo anaphunzitsabe anthu nzeru; inde, anatchera makutu nafunafuna nalongosola miyambi yambiri.

10 Mlalikiyo anasanthula akapeze mau okondweretsa, ndi zolemba zoongoka ngakhale mau oona.

11 Mau a anzeru akunga zisonga, omwe akundika mau amene mbusa mmodzi awapatsa mau ao akunga misomali yokhomedwa zolimba.

12 Pamodzi ndi izi, mwananga, tachenjezedwa; pakuti saleka kulemba mabuku ambiri; ndipo kuphunzira kwambiri kutopetsa thupi.

13 Mau atha; zonse zamveka zatha; opa Mulungu, musunge malamulo ake; pakuti choyenera anthu onse ndi ichi.

14 Pakuti Mulungu adzanena mlandu wa zochita zonse, ndi zobisika zonse, ngakhale zabwino ngakhale zoipa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ECC/12-41e9d6ebfa30c06b056356f986dcc7b0.mp3?version_id=1068—