Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 20

1 Vinyo achita chiphwete, chakumwa chaukali chisokosa;

wosochera nazo alibe nzeru.

2 Kuopsa kwa mfumu ndiko kubangula kwa mkango;

womputa achimwira moyo wakewake.

3 Kuli ulemu kwa mwamuna kupewa ndeu;

koma zitsiru zonse zimangokangana.

4 Waulesi salima chifukwa cha chisanu;

adzapemphapempha m’masika osalandira kanthu.

5 Uphungu wa m’mtima mwa munthu ndiwo madzi akuya;

koma munthu wozindikira adzatungapo.

6 Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwake;

koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?

7 Wolungama woyenda mwangwiro,

anake adala pambuyo pake.

8 Mfumu yokhala pa mpando woweruzira

ipirikitsa zoipa zonse ndi maso ake.

9 Ndani anganene, Ndasambitsa mtima wanga,

ndayera opanda tchimo?

10 Miyeso yosiyana, ndi malichero osiyana,

zonse ziwirizi zinyansa Yehova.

11 Ngakhale mwana adziwika ndi ntchito zake;

ngati ntchito yake ili yoyera ngakhale yolungama.

12 Khutu lakumva, ndi diso lopenya,

Yehova anapanga onse awiriwo.

13 Usakonde tulo ungasauke;

phenyula maso, udzakhuta zakudya.

14 Wogula ati, Chachabe chimenecho,

koma atachoka adzitama.

15 Alipo golide ndi ngale zambiri;

koma milomo yodziwa ndiyo chokometsera cha mtengo wapatali.

16 Tenga malaya a woperekera mlendo chikole;

woperekera mkazi wachilendo chikole umgwire mwini.

17 Zakudya za chinyengo zikondweretsa munthu;

koma pambuyo pake m’kamwa mwake mudzadzala tinsangalabwi.

18 Uphungu utsimikiza zolingalira,

ponya nkhondo utapanga upo.

19 Kazitape woyendayenda awanditsa zinsinsi;

usadudukire woyasama milomo yake.

20 Wotemberera atate wake ndi amake,

nyali yake idzazima mu mdima woti bii.

21 Cholowa chingalandiridwe msangamsanga poyamba pake;

koma chitsiriziro chake sichidzadala.

22 Usanene, Ndidzabwezera zoipa;

yembekeza Yehova, adzakupulumutsa.

23 Miyeso yosiyana inyansa Yehova,

ndi mulingo wonyenga suli wabwino.

24 Yehova alongosola mayendedwe a mwamuna;

munthu tsono angazindikire bwanji njira yake?

25 Kunena mwansontho, Ichi nchopatulika,

kuli msampha kwa munthu,

ndi kusinkhasinkha pambuyo pake atawinda.

26 Mfumu yanzeru ipeta amphulupulu,

niyendetsapo njinga ya galeta.

27 Mzimu wa munthu ndiwo nyali ya Yehova;

usanthula m’kati monse mwa mimba.

28 Chifundo ndi ntheradi zisunga mfumu;

chifundo chichirikiza mpando wake.

29 Ulemerero wa anyamata ndiwo mphamvu yao;

kukongola kwa nkhalamba ndi imvi.

30 Mikwingwirima yopweteka ichotsa zoipa;

ndi mikwapulo ilowa m’kati mwa mimba.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/20-2b43d7887d7b72d12907ad946cec2411.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 21

1 Mtima wa mfumu uli m’dzanja la Yehova ngati mitsinje ya madzi;

aulozetsa komwe afuna.

2 Njira zonse za munthu zilungama pamaso pake;

koma Yehova ayesa mitima.

3 Kuchita chilungamo ndi chiweruzo

kupambana ndi nsembe kumkonda Yehova.

4 Maso akunyada, ndi mtima wodzikuza,

ndi nyali ya oipa, zili tchimo.

5 Zoganizira za wakhama zichulukitsadi katundu;

koma yense wansontho angopeza umphawi.

6 Kupata chuma ndi lilime lonama

ndiko nkhungu yoyendayenda, ngakhale misampha ya imfa.

7 Chiwawa cha amphulupulu chidzawakokolola;

chifukwa akana kuchita chiweruzo.

8 Wosenza tchimo njira yake ikhotakhota;

koma ntchito ya woyera mtima ilungama.

9 Kukhala pangodya ya tsindwi kufunika

kuposa kukhala m’nyumba ndi mkazi wolongolola.

10 Wamphulupulu mtima wake umkhumba zoipa;

sakomera mtima mnzake.

11 Polangidwa wonyoza, wachibwana alandira nzeru,

naphunzira pakuyang’ana pa wanzeru.

12 Wolungama aganizira za nyumba ya wamphulupulu,

kuti amphulupulu amagwetsedwa, naona zoipa.

13 Wotseka makutu ake polira waumphawi,

nayenso adzalira koma osamvedwa.

14 Mphatso ya m’tseri ipembedza mkwiyo,

ndi mtulo wa pamfunga ukali wolimba.

15 Kuchita chiweruzo kukondweretsa wolungama;

koma kuwaononga akuchita mphulupulu.

16 Munthu wosochera panjira ya nzeru

adzakhala m’msonkhano wa akufa.

17 Wokonda zoseketsa adzasauka;

wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

18 Wochimwa ndiye chiombolo cha wolungama;

ndipo wachiwembu adzalowa m’malo mwa oongoka mtima.

19 Kukhala m’chipululu kufunika

kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wong’ung’udza.

20 Mokhala wanzeru muli katundu wofunika ndi mafuta;

koma wopusa angozimeza.

21 Wolondola chilungamo ndi chifundo

apeza moyo, ndi chilungamo, ndi ulemu.

22 Wanzeru akwera pa mzinda wa olimba,

nagwetsa mphamvu yake imene anaikhulupirira.

23 Wosunga m’kamwa mwake ndi lilime lake

asunga moyo wake kumavuto.

24 Wonyada wodzikuza dzina lake ndiye wonyoza;

achita mwaukali modzitama.

25 Chifuniro cha waulesi chimupha;

chifukwa manja ake akana kugwira ntchito.

26 Ena asirira modukidwa tsiku lonse;

koma wolungama amapatsa osamana.

27 Nsembe ya oipa inyansa;

makamaka pakudza nayo iwo mwachiwembu.

28 Mboni yonama idzafa;

koma mwamuna wakumvetsa adzanena mosakayika.

29 Munthu woipa aumitsa nkhope yake;

koma woongoka mtima akonza njira zake.

30 Kulibe nzeru ngakhale luntha

ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

31 Kavalo amakonzedweratu chifukwa cha tsiku la nkhondo;

koma wopulumutsa ndiye Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/21-bf18b07f5d70f5c7c7a8eabca72c35d8.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 22

1 Mbiri yabwino ifunika kopambana chuma chambiri;

kukukomera mtima anzako kuposasilivandi golide.

2 Wolemera ndi wosauka akumana,

wolenga onsewo ndiye Yehova.

3 Wochenjera aona zoipa, nabisala;

koma achibwana angopitirira, nalipitsidwa.

4 Mphotho ya chifatso ndi kuopa Yehova

ndiye chuma, ndi ulemu, ndi moyo.

5 Minga ndi misampha ili m’njira ya wokhota;

koma wosunga moyo wake adzatalikira imeneyo.

6 Phunzitsa mwana poyamba njira yake;

ndipo angakhale atakalamba sadzachokamo.

7 Wolemera alamulira osauka;

ndipo wokongola ndiye kapolo wa womkongoletsa.

8 Wofesa zosalungama adzakolola tsoka;

ndipo nthyole ya mkwiyo wake idzalephera.

9 Mwini diso lamataya adzadala;

pakuti apatsa osauka zakudya zake.

10 Ukainga wonyoza, makangano adzatuluka;

makani ndi manyazi adzalekeka.

11 Wokonda kuyera mtima,

mfumu idzakhala bwenzi lake

chifukwa cha chisomo cha milomo yake.

12 Maso a Yehova atchinjiriza wodziwa;

koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.

13 Waulesi ati, Pali mkango panjapo,

ndidzaphedwa pamakwalalapo.

14 M’kamwa mwa mkazi wachiwerewere muli dzenje lakuya;

yemwe Yehova amkwiyira adzagwamo.

15 Utsiru umangidwa mumtima mwa mwana;

koma nthyole yomlangira idzauingitsira kutali.

16 Wotsendereza waumphawi kuti achulukitse chuma chake,

ndi wopatsa wolemera kanthu, angosauka.

Malangizo a pa makhalidwe oyenera munthu

17 Tchera makutu ako, numvere mau a anzeru,

nulozetse mtima wako kukadziwa zanga.

18 Pakuti mauwo akondweretsa ngati uwasunga m’kati mwako,

ngati akhazikika pamodzi pa milomo yako.

19 Ndakudziwitsa amenewo lero, ngakhale iwedi,

kuti ukhulupirire Yehova.

20 Kodi sindinakulembere zoposa

za uphungu ndi nzeru;

21 kuti ukadziwitse ntheradi yake ya mau oona,

nukabwere ndi mau oona kwa iwo amene anakutumiza?

22 Usalande za waumphawi chifukwa ali waumphawi,

ngakhale kutsendereza wosauka kubwalo.

23 Pakuti Yehova adzanenera mlandu wao;

omwe akwatula zao Iye adzakwatula moyo wao.

24 Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga;

ngakhale kupita ndi mwamuna waukali;

25 kuti ungaphunzire mayendedwe ake,

ndi kutengera moyo wako msampha.

26 Usakhale wodulirana mpherere,

ngakhale kumperekera chikole cha ngongole zake.

27 Ngati ulibe chobwezera

kodi achotserenji kama lako pansi pako?

28 Usasunthe chidziwitso chakale cha m’malire,

chimene makolo ako anachiimika.

29 Kodi upenya munthu wofulumiza ntchito zake?

Adzaima pamaso pa mafumu, osaima pamaso pa anthu achabe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/22-5349935a35273ed6009f979506c51d4f.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 23

1 Pamene ukhala ulinkudya ndi mkulu,

zikumbukira ameneyo ali pamaso pako;

2 nuike mpeni pakhosi pako,

ngati uli wadyera.

3 Usakhumbe zolongosoka zake;

pokhala zakudya zonyenga.

4 Usadzitopetse kuti ulemere;

leka nzeru yakoyako.

5 Kodi upenyeranji chimene kulibe?

Pakuti chuma chimera mapiko,

ngati mphungu youluka mumlengalenga.

6 Usadye zakudya zake za wa maso ankhwenzule,

ngakhale kukhumba zolongosoka zake.

7 Pakuti monga asinkha m’kati mwake, ali wotere;

ati kwa iwe, Idya numwe;

koma mtima wake suli pa iwe.

8 Pakuti nthongo imene unaidya udzaisanza,

ndi kutaya mau ako okondweretsa.

9 Usalankhule m’makutu a wopusa;

pakuti adzapeputsa nzeru ya mau ako.

10 Usasunthe chidziwitso chakale cha m’malire;

ngakhale kulowa m’minda ya amasiye;

11 pakuti Mombolo wao walimba;

adzawanenera mlandu wao pa iwe.

12 Lozetsa mtima wako kumwambo,

ndi makutu ako ku mau anzeru.

13 Usamane mwana chilango;

pakuti ukammenya ndi nthyole safa ai.

14 Udzammenya ndi nthyole,

nudzapulumutsa moyo wake kunsi kwa manda.

15 Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru,

mtima wanga wa inedi udzakondwa.

16 Imso zanga zidzasangalala,

polankhula milomo yako zoongoka.

17 Mtima wako usachitire nsanje akuchimwawo;

koma opabe Yehova tsiku lonse.

18 Pakutitu padzakhala mphotho;

ndipo chiyembekezo chako sichidzalephereka.

19 Tamvera tsopano, mwananga, utenge nzeru,

ulunjikitse mtima wako m’njiramo.

20 Usakhale mwa akumwaimwa vinyo,

ndi ankhuli osusuka.

21 Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka;

ndipo kusinza kudzaveka munthu nsanza.

22 Tamvera atate wako anakubala,

usapeputse amai ako atakalamba.

23 Gula ntheradi, osaigulitsa;

nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.

24 Atate wa wolungama adzasekeradi;

wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25 Atate wako ndi amai ako akondwere,

amai ako akukubala asekere.

26 Mwananga, undipatse mtima wako,

maso ako akondwere ndi njira zanga.

27 Pakuti mkazi wadama ndiye dzenje lakuya;

ndipo mkazi wachiwerewere ndiye mbuna yopapatiza.

28 Pakuti abisalira ngati wachifwamba,

nachulukitsa anthu a chiwembu.

29 Ndani ali ndi chisoni? Ndani asauka?

Ndani ali ndi makangano? Ndani ang’ung’udza?

Ndani alasidwa chabe? Ndani afiira maso?

30 Ngamene achedwa pali vinyo,

napita kukafunafuna vinyo wosakanizidwa.

31 Usayang’ane pavinyo alikufiira,

alikung’azimira m’chikho,

namweka mosalala.

32 Pa chitsiriziro chake aluma ngati njoka,

najompha ngati mamba.

33 Maso ako adzaona zachilendo,

mtima wako udzalankhula zokhota.

34 Udzafanana ndi wina wogona pakati pa nyanja,

pena wogona pansonga ya mlongoti wa ngalawa.

35 Udzati, Anandimenya, osaphwetekedwa ine;

anandikwapula, osamva ine;

ndidzauka nthawi yanji?

Ndidzafunafunanso vinyoyo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/23-31ad928ab24bdf4ab95ef06141cbdc8d.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 24

1 Usachitire nsanje anthu oipa,

ngakhale kufuna kukhala nao;

2 pakuti mtima wao ulingalira za chionongeko;

milomo yao ilankhula za mphulupulu.

3 Nzeru imangitsa nyumba;

luntha liikhazikitsa.

4 Kudziwa kudzaza zipinda zake

ndi chuma chonse chofunika cha mtengo wake.

5 Mwamuna wanzeru ngwamphamvu;

munthu wodziwa ankabe nalimba.

6 Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo,

ndi kupulumuka pochuluka aphungu.

7 Nzeru italikira chitsiru;

satsegula pakamwa kubwalo.

8 Wolingalira zakuchita zoipa

anthu adzamtcha wachiwembu.

9 Maganizo opusa ndiwo tchimo;

wonyoza anyansa anthu.

10 Ukalefuka tsiku la tsoka

mphamvu yako ichepa.

11 Omwe atengedwa kuti akafe, uwapulumutse;

omwe ati aphedwe, usaleke kuwalanditsa.

12 Ukanena, Taonani, sitinadziwe chimenechi;

kodi woyesa mitima sachizindikira ichi?

Ndi wosunga moyo wako kodi sachidziwa?

Ndipo kodi sabwezera munthu yense

monga mwa machitidwe ake?

13 Mwananga, idya uchi pakuti ngwabwino,

ndi chisa chake chitsekemera m’kamwa mwako.

14 Potero udzadziwa kuti nzeru ili yotero m’moyo wako;

ngati waipeza padzakhala mphotho,

ndipo chiyembekezo chako sichidzalephereka.

15 Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;

usapasule popuma iyepo.

16 Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso;

koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.

17 Usakondwere pakugwa mdani wako;

mtima wako usasekere pokhumudwa iye;

18 kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa,

ndi kuleka kumkwiyira.

19 Usavutike mtima chifukwa cha ochita zoipa;

ngakhale kuchitira nsanje amphulupulu.

20 Pakuti woipayo sadzalandira mphotho;

nyali ya amphulupulu idzazima.

21 Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe,

osadudukira anthu osinthasintha.

22 Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka;

ndipo ndani adziwa chionongeko cha zaka zao?

23 Izinso zili za anzeru,

poweruza chetera silili labwino.

24 Wonena kwa woipa, Wolungama iwe;

magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira.

25 Omwe amdzudzula adzasekera,

nadzadalitsika ndithu.

26 Wobwezera mau oongoka

apsompsona milomo.

27 Longosola ntchito yako panjapo, nuikonzeretu kumunda;

pambuyo pake ndi kumanga nyumba yako.

28 Usachitire mnzako umboni womtsutsa opanda chifukwa;

kodi udzanyenga ndi milomo yako?

29 Usanene, Ndidzamchitira zomwezo anandichitira ine

ndidzabwereza munthuyo monga mwa machitidwe ake.

30 Ndinapita pamunda wa waulesi,

polima mphesa munthu wosowa nzeru.

31 Taonani, ponsepo panamera minga,

ndi kuwirirapo khwisa;

tchinga lake lamiyala ndi kupasuka.

32 Pamenepo ndinayang’ana ndi kuganizira,

ndinaona ndi kulandira mwambo.

33 Tulo tapang’ono, kungoodzera pang’ono,

kungomanga manja pang’ono m’kugona,

34 ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala;

ndi kusauka kwako ngati munthu wachikopa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/24-d041c432688e739b0966df167545db65.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 25

Miyambo ya Solomoni yosonkhanitsa nthawi ya Hezekiya

1 Iyinso ndiyo miyambo ya Solomoni

imene anthu a Hezekiya mfumu ya Yuda anailemba.

2 Kubisa kanthu ndi ulemerero wa Mulungu;

koma ulemerero wa mafumu ndi kusanthula kanthu.

3 Pamlengalenga patalika, ndi padziko pakuya,

koma mitima ya mafumu singasanthulike.

4 Chotserasilivamphala yake,

mmisiri wa ng’anjo atulutsamo mbale.

5 Chotsera woipa pamaso pa mfumu,

mpando wake udzakhazikika m’chilungamo.

6 Usadzitame pamaso pa mfumu,

ngakhale kuima m’malo mwa akulu.

7 Pakuti kunena kwa iwe, Takwera kuno,

kupambana ndi kuti utsitsidwe pamaso pa kalonga,

amene maso ako anamuona.

8 Usatuluke mwansontho kukalimbana,

ungalephere pa kutha kwake,

atakuchititsa mnzako manyazi.

9 Nena mlandu wako ndi mnzako,

osawulula zinsinsi za mwini;

10 kuti wakumva angakutonze,

mbiri yako yoipa ndi kusachoka.

11 Mau oyenera a pa nthawi yake

akunga zipatso zagolide m’nsengwa zasiliva.

12 Monga mphete yagolide ndi chipini chagolide woyengeka,

momwemo wanzeru wodzudzula pa khutu lomvera.

13 Monga chisanu cha chipale chofewa pa nthawi ya masika,

momwemo mthenga wokhulupirika kwa amene anamtuma;

atsitsimutsa moyo wa ambuyake.

14 Monga mitambo ndi mphepo popanda mvula,

momwemo ndiye wodzikweza ndi zipatso zake monyenga.

15 Chipiriro chipembedza mkulu;

lilime lofatsa lithyola fupa.

16 Wapeza uchi kodi? Idyapo wokwanira,

kuti ungakukole, nusanze.

17 Phazi lako lilowe m’nyumba ya mnzako kamodzikamodzi;

kuti angatope nawe ndi kukuda.

18 Wochitira mnzake umboni wonama

ndiye chibonga, ndi lupanga, ndi muvi wakuthwa.

19 Kukhulupirira munthu wa chiwembu tsiku latsoka

kunga dzino lothyoka ndi phazi loguluka.

20 Monga wovula malaya tsiku lamphepo,

ngakhale kuthira vinyo wosasa m’soda,

momwemo woimbira nyimbo munthu wachisoni.

21 Mdani wako akamva njala umdyetse,

akamva ludzu ummwetse madzi.

22 Pakuti udzaunjika makala amoto pamutu pake;

ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.

23 Mphepo ya kumpoto ifikitsa mvula;

chomwecho lilime losinjirira likwiyitsa nkhope.

24 Kukhala pangodya ya tsindwi kufunika

kuposa kukhala m’nyumba ndi mkazi wolongolola.

25 Monga madzi ozizira kwa munthu wotopa,

momwemo mau abwino akuchokera kudziko lakutali.

26 Monga kasupe wopondedwa, ndi chitsime choonongeka,

momwemo wolungama ngati agonjera woipa.

27 Kudya uchi wambiri sikuli kwabwino;

chomwecho kufunafuna ulemu wakowako sikuli ulemu.

28 Wosalamulira mtima wake

akunga mzinda wopasuka wopanda linga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/25-40ef2cfb514d1d550f773dc0220cfe21.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 26

1 Monga chipale chofewa m’malimwe, ndi mvula m’masika,

momwemo ulemu suyenera chitsiru.

2 Monga mpheta ilikuzungulira, ndi namzeze alikuuluka,

momwemo temberero la pachabe silifikira.

3 Chikoti chiyenera kavalo, ndi cham’kamwa chiyenera bulu,

ndi nthyole iyenera pamsana pa zitsiru.

4 Usayankhe chitsiru monga mwa utsiru wake,

kuti ungafanane nacho iwe wekha.

5 Yankha chitsiru monga mwa utsiru wake,

kuti asadziyese wanzeru.

6 Wotumiza mau ndi dzanja la chitsiru

adula mapazi ake, namwa zompweteka.

7 Miyendo ya wopunduka ili yolobodoka,

momwemo mwambi m’kamwa mwa zitsiru.

8 Monga thumba la ngale m’mulu wa miyala,

momwemo wochitira chitsiru ulemu.

9 Monga munga wolasa dzanja la woledzera,

momwemo mwambi m’kamwa mwa zitsiru.

10 Monga woponya mivi ndi kulasa onse,

momwemo wolembera chitsiru,

ndi wolembera omwe alikupita panjira.

11 Monga galu abweranso kumasanzi ake,

momwemo chitsiru chichitanso zopusa zake.

12 Kodi uona munthu wodziyesa wanzeru?

Ngakhale chitsiru chidzachenjera koma ameneyo ai.

13 Waulesi ati, Mkango uli panjira,

wobangulawo uli m’makwalala.

14 Monga chitseko chikankhikira pa zitsulo za pamphuthu,

momwemo waulesi agubuduka pakama pake.

15 Waulesi alonga dzanja lake m’mbale;

kumtopetsa kulibweza kukamwa kwake.

16 Waulesi adziyesa wanzeru

koposa anthu asanu ndi awiri akuyankha mozindikira.

17 Wakungopita ndi kuvutika ndi ndeu yosakhala yake

akunga wogwira makutu a galu.

18 Monga woyaluka woponya nsakali,

mivi, ndi imfa,

19 momwemo wonyenga mnzake ndi kuti,

ndi kusewera kumeneku.

20 Posowa nkhuni moto ungozima;

ndi popanda kazitape makangano angoleka.

21 Monga makala ozizira pa makala akunyeka,

ndi nkhuni pamoto;

momwemo munthu wamakangano autsa ndeu.

22 Mau a kazitape ndi zakudya zolongosoka

zitsikira m’kati mwa mimba.

23 Milomo yofunitsitsa ndi mtima woipa

ikunga mbale yadothi anaimata ndi mphala yasiliva.

24 Wakuda mnzake amanyenga ndi milomo yake;

koma akundika chinyengo m’kati mwake.

25 Pamene akometsa mau ake usamkhulupirire;

pakuti m’mtima mwake muli zonyansa zisanu ndi ziwiri.

26 Angakhale abisa udani wake pochenjera,

koma udyo wake udzavumbulutsidwa posonkhana anthu.

27 Wokumba dzenje adzagwamo,

wogubuduza mwala, udzabweranso pa iye mwini.

28 Lilime lonama lida omwewo linawasautsa;

ndipo m’kamwa mosyasyalika mungoononga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/26-5c6ccb3e673edac2f1b7f6d743fb9f2d.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 27

1 Usanyadire zamawa,

popeza sudziwa tsiku lina lidzabala chiyani?

2 Wina akutume, si m’kamwa mwako ai;

mlendo, si milomo ya iwe wekha.

3 Mwala ulemera, mchenga ndiwo katundu;

koma mkwiyo wa chitsiru upambana kulemera kwake.

4 Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka;

koma ndani angalakike ndi nsanje?

5 Chidzudzulo chomveka chiposa chikondi chobisika.

6 Kulasa kwa bwenzi kuli kokhulupirika;

koma mdani apsompsona kawirikawiri.

7 Mtima wokhuta upondereza chisa cha uchi;

koma wakumva njala ayesa zowawa zonse zotsekemera.

8 Monga mbalame yosochera kuchisa chake,

momwemo munthu wosochera kumalo ake.

9 Mafuta ndi zonunkhira zikondweretsa mtima,

ndi ubwino wa bwenzi uteronso pakupangira uphungu.

10 Mnzako, ndi mnzake wa atate wako, usawasiye;

usanke kunyumba ya mbale wako tsiku la tsoka lako;

mnansi wapafupi aposa mbale wakutali.

11 Mwananga, khala wanzeru, nukondweretse mtima wanga;

kuti ndimuyankhe yemwe anditonza.

12 Wochenjera aona zoipa, nabisala;

koma achibwana angopitirira, nalipitsidwa.

13 Tenga malaya a woperekera mlendo chikole;

woperekera mkazi wachiwerewere chikole umgwire mwini.

14 Yemwe adalitsa mnzake ndi mau aakulu pouka mamawa,

anthu adzachiyesa chimenecho temberero.

15 Kudonthadontha tsiku lamvula,

ndi mkazi wolongolola ali amodzimodzi.

16 Wofuna kumletsayo afuna kuletsa mphepo;

dzanja lake lamanja lingogwira mafuta.

17 Chitsulo chinola chitsulo;

chomwecho munthu anola nkhope ya mnzake.

18 Wosunga mkuyu adzadya zipatso zake;

wosamalira ambuyake adzalemekezedwa.

19 Monga m’madzi nkhope zionana,

momwemo mitima ya anthu idziwana.

20 Kunsi kwa manda ndi kuchionongeko sikukhuta;

ngakhale maso a munthu sakhutai.

21 Silivaasungunuka m’mbiya,

ndi golide m’ng’anjo,

motero chomwe munthu achitama adziwika nacho.

22 Ungakhale ukonola chitsiru m’mtondo ndi munsi, pamodzi ndi mphale,

koma utsiru wake sudzamchoka.

23 Udziwitsitse zoweta zako zili bwanji,

samalira magulu ako;

24 pakuti chuma sichili chosatha;

kodi korona alipobe mpaka mibadwomibadwo.

25 Amatuta udzu, msipu uoneka,

atchera masamba a kumapiri.

26 Anaankhosa akuveka,

atonde aombolera munda;

27 mkaka wa mbuzi udzakukwanira kudya;

ndi a pa banja lako ndi adzakazi ako.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/27-622317ae4643f2833d73206325c895f5.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 28

Mau olinganiza zosiyana

1 Woipa athawa palibe momthamangitsa;

koma olungama alimba mtima ngati mkango.

2 Pochimwa dziko akalonga ake achuluka;

koma anthu ozindikira ndi odziwa

alikhazikikitsa nthawi yaikulu.

3 Munthu waumphawi wotsendereza osauka

akunga mvula yamadzi yokokolola dzinthu.

4 Omwe asiya chilamulo atama oipa;

koma omwe asunga chilamulo akangana nao.

5 Oipa samvetsetsa chiweruzo;

koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

6 Waumphawi woyenda mwangwiro

apambana ndi yemwe akhotetsa njira zake, angakhale alemera.

7 Wosunga chilamulo ndiye mwana wozindikira;

koma mnzao wa adyera achititsa atate wake manyazi.

8 Wochulukitsa chuma chake, pokongoletsa ndi phindu,

angokundikira yemwe achitira osauka chisoni.

9 Wopewetsa khutu lake kuti asamve chilamulo,

ngakhale pemphero lake linyansa.

10 Wosocheretsa oongoka mtima alowe m’njira yoipa,

adzagwa mwini m’dzenje lake;

koma angwiro adzalandira cholowa chabwino.

11 Wolemera adziyesa wanzeru;

koma wosauka wozindikira aululitsa zake.

12 Posekera olungama pali ulemerero wambiri;

koma pouka oipa anthu amabisala.

13 Wobisa machimo ake sadzaona mwai;

koma wakuwavomereza, nawasiya adzachitidwa chifundo.

14 Wodala munthu wakuopa kosalekeza;

koma woumitsa mtima wake adzagwa m’zoipa.

15 Monga mkango wobangula ndi chilombo choyendayenda,

momwemo mfumu yoipa ya anthu osauka.

16 Kalonga wosowa nzeru apambana kusautsa;

koma yemwe ada chisiriro adzatanimphitsa moyo wake.

17 Wopalamula mlandu wakupha munthu adzathawira kudzenje;

asamuletse.

18 Woyenda mwangwiro adzapulumuka;

koma wokhota m’mayendedwe ake adzagwa posachedwa.

19 Wolima munda wake zakudya zidzamkwanira;

koma wotsata anthu opanda pake umphawi udzamkwanira.

20 Munthu wokhulupirika ali ndi madalitso ambiri;

koma wokangaza kulemera sadzapulumuka chilango.

21 Chetera silili labwino,

ngakhale kulakwa kuti ukadye kanthu.

22 Mwini diso lankhwenzule akangaza kulemera,

osadziwa kuti umphawi udzamfikira.

23 Adzamkomera mtima wodzudzula m’tsogolo mwake,

koposa wosyasyalika ndi lilime lake.

24 Wobera atate wake, pena amake, nati, Palibe kulakwa;

ndiye mnzake wa munthu wopasula.

25 Wodukidwa mtima aputa makangano;

koma wokhulupirira Yehova adzakula.

26 Wokhulupirira mtima wakewake ali wopusa;

koma woyenda mwanzeru adzapulumuka.

27 Wogawira aumphawi sadzasowa;

koma wophimba maso ake adzatembereredwa kwambiri.

28 Pouka oipa anthu amabisala;

koma pakufa amenewo olungama achuluka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/28-9657f1c463c151f413bb32405a142b8a.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 29

1 Yemwe aumitsa khosi atadzudzulidwa kwambiri,

adzasweka modzidzimuka, palibe chomchiritsa.

2 Pochuluka olungama anthu akondwa;

koma polamulira woipa anthu ausa moyo.

3 Mwamuna wokonda nzeru akondweretsa atate wake;

koma wotsagana ndi akazi adama amwaza chuma.

4 Mfumu akhazikitsa dziko ndi chiweruzo;

koma wosonkhetsa anthu mphatso alipululutsa.

5 Wosyasyalika mnzake

atcherera mapazi ake ukonde.

6 M’kulakwa kwa woipa muli msampha;

koma wolungama aimba, nakondwera.

7 Wolungama asamalira mlandu wa osauka;

koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.

8 Anthu onyoza atentha mzinda;

koma anzeru alezetsa mkwiyo.

9 Munthu wanzeru akatsutsana ndi munthu wopusa,

ngakhale akwiya, ngakhale aseka, palibe mtendere.

10 Anthu ankhanza ada wangwiro;

koma oongoka mtima asamalira moyo wake.

11 Chitsiru chivumbulutsa mkwiyo wake wonse;

koma wanzeru auletsa nautontholetsa.

12 Mkulu akamvera chinyengo,

atumiki ake onse ali oipa.

13 Waumphawi ndi wotsendereza akumana;

Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.

14 Mfumu yolamulira osauka mwantheradi,

mpando wake udzakhazikika kufikira nthawi zonse.

15 Nthyole ndi chidzudzulo zipatsa nzeru;

koma mwana womlekerera achititsa amake manyazi.

16 Pochuluka oipa zolakwa zichuluka;

koma olungama adzaona kugwa kwao.

17 Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa;

nadzasangalatsa moyo wako.

18 Popanda chivumbulutso anthu amasauka;

koma wosunga chilamulo adalitsika.

19 Kapolo sangalangizidwe ndi mau,

pakuti azindikira koma osavomera.

20 Kodi uona munthu wansontho m’mau ake?

Ngakhale chitsiru chidzachenjera, koma ameneyo ai.

21 Yemwe alera kapolo wake mwa ufulu kuyambira ubwana wake,

pambuyo pake adzadziyesa mwana wobala.

22 Mwamuna wamkwiyo aputa makangano;

waukali achuluka zolakwa.

23 Kudzikuza kwa munthu kudzamchepetsa;

koma wokhala ndi mtima wodzichepetsa adzalemekezedwa.

24 Woyenda ndi mbala ada moyo wakewake;

amva kulumbira, koma osawulula kanthu.

25 Kuopa anthu kutchera msampha;

koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka.

26 Ambiri afunafuna chiyanjano cha mkulu;

koma chiweruzo cha munthu chichokera kwa Yehova.

27 Munthu woipa anyansa olungama;

ndipo woongoka m’njira anyansa wochimwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/29-e0e661a79b323b61f7b9284f54a3320d.mp3?version_id=1068—