Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 10

Miyambo yosiyanasiyana

Miyambo ya Solomoni:

1 Mwana wanzeru akondweretsa atate;

koma mwana wopusa amvetsa amake chisoni.

2 Chuma cha uchimo sichithangata;

koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.

3 Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;

koma amainga chifuniro cha wochimwa.

4 Wochita ndi dzanja laulesi amasauka;

koma dzanja la akhama lilemeretsa.

5 Wokolola m’malimwe ndi mwana wanzeru;

koma wogona pakututa ndi mwana wochititsa manyazi.

6 Madalitso ali pamutu pa wolungama;

koma m’kamwa mwa oipa mubisa chiwawa.

7 Amayesa wolungama wodala pomkumbukira;

koma dzina la oipa lidzavunda.

8 Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;

koma chitsiru cholongolola chidzagwa.

9 Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;

koma wokhotetsa njira zake adzadziwika.

10 Wotsinzinira achititsa chisoni;

koma wodzudzula momveka achita mtendere.

11 M’kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;

koma m’kamwa mwa oipa mubisa chiwawa.

12 Udani upikisanitsa;

koma chikondi chikwirira zolakwa zonse.

13 Nzeru ipezedwa m’milomo ya wozindikira;

koma wopusa pamsana pake nthyole.

14 Anzeru akundika zomwe adziwa;

koma m’kamwa mwa chitsiru muononga tsopano lino.

15 Chuma cha wolemera ndi mzinda wake wolimba;

koma umphawi wao uononga osauka.

16 Ntchito za wolungama zipatsa moyo;

koma phindu la oipa lichimwitsa.

17 Wosunga mwambo ali m’njira ya moyo;

koma wosiya chidzudzulo asochera.

18 Wobisa udani ali ndi milomo yonama;

wonena ugogodi ndiye chitsiru.

19 Pochuluka mau zolakwa sizisoweka;

koma wokhala chete achita mwanzeru.

20 Lilime la wolungama likungasilivawosankhika;

koma mtima wa oipa uli wachabe.

21 Milomo ya wolungama imadyetsa ambiri;

koma zitsiru zimafa posowa nzeru.

22 Madalitso a Yehova alemeretsa,

saonjezerapo chisoni.

23 Masewero a chitsiru ndiwo kuchita zoipa;

koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

24 Chomwe woipa achiopa chidzamfikira;

koma chomwe olungama achifuna chidzapatsidwa.

25 Monga kavumvulu angopita, momwemo woipa kuli zii;

koma olungama ndiwo maziko osatha.

26 Ngati vinyo wowawa m’mano, ndi utsi m’maso,

momwemo waulesi kwa iwo amene amtuma.

27 Kuopa Yehova kutanimphitsa masiku;

koma zaka za oipa zidzafinimpha.

28 Chiyembekezo cha olungama ndicho chimwemwe;

koma chidikiro cha oipa chidzaonongeka.

29 Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima;

koma akuchita zoipa adzaonongeka.

30 Wolungama sadzachotsedwa konse;

koma oipa sadzakhalabe m’dziko.

31 M’kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru;

koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32 Milomo ya wolungama idziwa zokondweretsa;

koma m’kamwa mwa oipa munena zokhota.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/10-6640647a67135114988aab0e34b398f7.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 11

1 Muyeso wonyenga unyansa Yehova;

koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

2 Pakudza kudzikuza padzanso manyazi;

koma nzeru ili ndi odzichepetsa.

3 Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera;

koma kukhota kwa achiwembu kudzawaononga.

4 Chuma sichithandiza tsiku la mkwiyo;

koma chilungamo chipulumutsa kuimfa.

5 Chilungamo cha wangwiro chimaongola njira yake;

koma woipa adzagwa ndi zoipa zake.

6 Chilungamo cha oongoka mtima chidzawapulumutsa;

koma achiwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.

7 Pomwalira woipa chidikiro chake chionongeka;

chiyembekezo cha uchimo chionongeka.

8 Wolungama apulumuka kuvuto;

woipa nalowa m’malo mwake.

9 Wonyoza Mulungu aononga mnzake ndi m’kamwa mwake;

koma olungama adzapulumuka pakudziwa.

10 Olungama akapeza bwino, mzinda usekera;

nufuula pakuonongeka oipa.

11 Madalitso a olungama akuza mzinda;

koma m’kamwa mwa oipa muupasula.

12 Wopeputsa mnzake asowa nzeru;

koma wozindikira amatonthola.

13 Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi;

koma wokhulupirika mtima abisa mau.

14 Popanda upo wanzeru anthu amagwa;

koma pochuluka aphungu pali chipulumutso.

15 Woperekera mlendo chikole adzaphwetekwapo;

koma wakuda chikole akhala ndi mtendere.

16 Mkazi wodekha agwiritsa ulemu;

aukali nagwiritsa chuma.

17 Wachifundo achitira moyo wake zokoma;

koma wankhanza avuta nyama yake.

18 Woipa alandira malipiro onyenga;

koma wofesa chilungamo aonadi mphotho.

19 Wolimbikira chilungamo alandira moyo;

koma wolondola zoipa adzipha yekha.

20 Okhota mtima anyansa Yehova;

koma angwiro m’njira zao amsekeretsa.

21 Zoonadi, wochimwa sadzapulumuka chilango;

koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.

22 Monga chipini chagolide m’mphuno ya nkhumba,

momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.

23 Chifuniro cha olungama chifikitsa zabwino zokha;

koma chiyembekezo cha oipa mkwiyo.

24 Alipo wogawira, nangolemerabe;

aliponso womana chomwe ayenera kupatsa nangosauka.

25 Mtima wa mataya udzalemera;

wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

26 Womana tirigu anthu amtemberera;

koma madalitso adzakhala pamutu pa wogulitsa.

27 Wopwaira ubwino afunitsa chikondwerero;

koma zoipa zidzamfikira wozilondola.

28 Wokhulupirira chuma chake adzagwa;

koma olungama adzaphuka ngati tsamba.

29 Wovuta banja lake adzalowa m’zomsautsa;

wopusa adzatumikira wanzeru.

30 Chipatso cha wolungama ndi mtengo wa moyo;

ndipo wokola mtima ali wanzeru.

31 Taonani, wolungama adzalandira mphotho kunja kuno;

koposa kotani woipa ndi wochimwa?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/11-3a2dfc12137683cdafeb18a644d55365.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 12

1 Wokonda mwambo akonda kudziwa;

koma wakuda chidzudzulo apulukira.

2 Yehova akomera mtima munthu wabwino;

koma munthu wa ziwembu amtsutsa.

3 Munthu sadzakhazikika ndi udyo,

muzu wa olungama sudzasunthidwa.

4 Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wake;

koma wochititsa manyazi akunga chovunditsa mafupa a mwamunayo.

5 Maganizo a olungama ndi chiweruzo;

koma uphungu wa oipa unyenga.

6 Mau a oipa abisalira mwazi;

koma m’kamwa mwa olungama muwalanditsa.

7 Oipa amagwa kuli zii;

koma banja la olungama limaimabe.

8 Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yake;

koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9 Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,

aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10 Wolungama asamalira moyo wa choweta chake;

koma chifundo cha oipa ndi nkhanza.

11 Zakudya zikwanira wolima minda yake;

koma wotsata anthu opanda pake asowa nzeru.

12 Woipa akhumba chokodwa ndi amphulupulu;

koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13 M’kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;

koma wolungama amatuluka m’mavuto.

14 Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m’kamwa mwake;

zochita za manja ake zidzabwezedwa kwa iye.

15 Njira ya chitsiru njolungama pamaso pakepake;

koma wanzeru amamvera uphungu.

16 Mkwiyo wa chitsiru udziwika posachedwa;

koma wanzeru amabisa manyazi.

17 Wolankhula ntheradi aonetsa chilungamo;

koma mboni yonama imanyenga.

18 Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;

koma lilime la anzeru lilamitsa.

19 Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse;

koma lilime lonama likhala kamphindi.

20 Chinyengo chili m’mitima ya oganizira zoipa;

koma aphungu a mtendere amakondwa.

21 Palibe vuto lidzagwera wolungama;

koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa.

22 Milomo yonama inyansa Yehova;

koma ochita ntheradi amsekeretsa.

23 Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa;

koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.

24 Dzanja la akhama lidzalamulira;

koma waulesi adzakhala ngati kapolo.

25 Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu;

koma mau abwino aukondweretsa.

26 Wolungama atsogolera mnzake;

koma njira ya oipa iwasokeretsa.

27 Waulesi samaotcha nyama yake anaigwira;

koma wolungama amalandira chuma chopambana cha anthu.

28 M’khwalala la chilungamo muli moyo;

m’njira ya mayendedwe ake mulibe imfa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/12-a208f60d659d30d94ba0fd02c30d5dc5.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 13

1 Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate;

koma wonyoza samvera chidzudzulo.

2 Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m’kamwa mwake;

koma moyo wa achiwembu udzadya chiwawa.

3 Wogwira pakamwa pake asunga moyo wake;

koma woyasamula milomo yake adzaonongeka.

4 Moyo wa waulesi ukhumba osalandira kanthu;

koma moyo wa akhama udzalemera.

5 Wolungama ada mau onama;

koma woipa anyansa, nadzichititsa manyazi.

6 Chilungamo chitchinjiriza woongoka m’njira;

koma udyo ugwetsa wochimwa.

7 Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu;

alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi chuma chambiri.

8 Chiombolo cha moyo wa munthu ndicho chuma chake;

koma wosauka samva chidzudzulo.

9 Kuunika kwa olungama kukondwa;

koma nyali ya oipa idzazima.

10 Kudzikuza kupikisanitsa;

koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

11 Chuma cholandiridwa mokangaza chidzachepa;

koma wokundika ndi dzanja adzaona zochuluka.

12 Chiyembekezo chozengereza chidwalitsa mtima;

koma pakufika chifunirocho ndicho mtengo wa moyo.

13 Wonyoza mau adziononga yekha;

koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

14 Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,

apatutsa kumisampha ya imfa.

15 Nzeru yabwino ipatsa chisomo;

koma njira ya achiwembu ili makolokoto.

16 Yense wochenjera amachita mwanzeru;

koma wopusa aonetsa utsiru.

17 Mthenga wolakwa umagwa m’zoipa;

koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.

18 Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa;

koma wolabadira chidzudzulo adzalemekezedwa.

19 Chifuniro chikondweretsa moyo chitachitidwa;

koma kusiya zoipa kunyansa opusa.

20 Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru:

koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

21 Zoipa zilondola ochimwa;

koma olungama adzalandira mphotho yabwino.

22 Wabwino asiyira zidzukulu zake cholowa chabwino;

koma wochimwa angosungira wolungama chuma chake.

23 M’kulima kwa osauka muli zakudya zambiri;

koma zinazo zimaonongeka posowa chiweruzo.

24 Wolekerera mwanake osammenya amuda;

koma womkonda amyambize kumlanga.

25 Wolungama adya nakhutitsa moyo wake;

koma mimba ya oipa idzasowa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/13-7e0058e913f39c50a46da6638a98fbd4.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 14

1 Mkazi yense wanzeru amanga banja lake;

koma wopusa alipasula ndi manja ake.

2 Woyenda moongoka mtima aopa Yehova;

koma wokhota m’njira yake amnyoza.

3 M’kamwa mwa chitsiru muli nthyole ya kudzikuza;

koma milomo ya anzeru idzawasunga.

4 Popanda zoweta modyera muti see;

koma mphamvu ya ng’ombe ichulukitsa phindu.

5 Mboni yokhulupirika siidzanama;

koma mboni yonyenga imalankhula zonama.

6 Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza;

koma wozindikira saona vuto m’kuphunzira.

7 Pita pamaso pa munthu wopusa,

sudzazindikira milomo yakudziwa.

8 Nzeru ya wochenjera ndiyo yakuti azindikire njira yake;

koma utsiru wa opusa ndiwo chinyengo.

9 Zitsiru zinyoza kupalamula;

koma mwa oongoka mtima muli chiyanjano.

10 Mtima udziwa kuwawa kwakekwake;

mlendo sadudukira ndi chimwemwe chake.

11 Nyumba ya oipa idzapasuka;

koma hema wa oongoka mtima adzakula.

12 Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;

koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

13 Ngakhale m’kuseka mtima uwawa;

ndipo matsiriziro a chiphwete ndi chisoni.

14 Wobwerera m’mbuyo m’mtima adzakhuta njira yake;

koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.

15 Wachibwana akhulupirira mau onse;

koma wochenjera asamalira mayendedwe ake.

16 Wanzeru amaopa nasiya zoipa;

koma wopusa amanyada osatekeseka.

17 Wokangaza kukwiya adzachita utsiru;

ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.

18 Achibwana amalandira cholowa cha utsiru;

koma ochenjera amavala nzeru ngati korona.

19 Oipa amagwadira abwino,

ndi ochimwa pa makomo a olungama.

20 Waumphawi adedwa ndi anzake omwe;

koma akukonda wolemera achuluka.

21 Wonyoza anzake achimwa;

koma wochitira osauka chifundo adala.

22 Kodi oganizira zoipa sasochera?

Koma akuganizira zabwino adzalandira chifundo ndi ntheradi.

23 M’ntchito zonse muli phindu;

koma kulankhulalankhula kungopatsa umphawi.

24 Korona wa anzeru ndi chuma chao;

utsiru wa opusa ndiwo utsiru.

25 Mboni yoona imalanditsa miyoyo;

koma wolankhula zonama angonyenga.

26 Wakuopa Yehova akhulupirira kolimba;

ndipo ana ake adzakhala ndi pothawirapo.

27 Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo,

kupatutsa kumisampha ya imfa.

28 Mu unyinji wa anthu muli ulemu wa mfumu;

koma popanda anthu kalonga aonongeka.

29 Wosakwiya msanga apambana kumvetsa;

koma wansontho akuza utsiru.

30 Mtima wabwino ndi moyo wa thupi;

koma nsanje ivunditsa mafupa.

31 Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wake;

koma wochitira wosauka chifundo amlemekeza.

32 Wochimwa adzakankhidwa m’kuipa kwake;

koma wolungama akhulupirirabe pomwalira.

33 Nzeru ikhalabe m’mtima wa wozindikira,

nidziwika pakati pa opusa.

34 Chilungamo chikuza mtundu wa anthu;

koma tchimo lichititsa fuko manyazi.

35 Mfumu ikomera mtima kapolo wochita mwanzeru;

koma idzakwiyira wochititsa manyazi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/14-9edb0598af40259cf8f0a0a5776b6b60.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 15

1 Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo;

koma mau owawitsa aputa msunamo.

2 Lilime la anzeru linena bwino zomwe adziwa;

koma m’kamwa mwa opusa mutsanulira utsiru.

3 Maso a Yehova ali ponseponse,

nayang’anira oipa ndi abwino.

4 Kuchiza lilime ndiko mtengo wa moyo;

koma likakhota liswa moyo.

5 Chitsiru chipeputsa mwambo wa atate wake;

koma wosamalira chidzudzulo amachenjera.

6 M’nyumba ya wolungama muli katundu wambiri;

koma m’phindu la woipa muli vuto.

7 Milomo ya anzeru iwanditsa nzeru,

koma mtima wa opusa suli wolungama.

8 Nsembe ya oipa inyansa Yehova;

koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.

9 Njira ya oipa inyansa Yehova;

koma akonda wolondola chilungamo.

10 Wosiya njira adzalangidwa mowawa;

wakuda chidzudzulo adzafa.

11 Kumanda ndi kuchionongeko kuli pamaso pa Yehova;

koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?

12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,

samapita kwa anzeru.

13 Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;

koma moyo umasweka ndi zowawa za m’mtima.

14 Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;

koma m’kamwa mwa opusa mudya utsiru.

15 Masiku onse a wosauka ali oipa;

koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.

16 Zapang’ono, ulikuopa Yehova,

zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso.

17 Kudya masamba, pali chikondano,

kuposa ng’ombe yonenepa pali udani.

18 Munthu wozaza aputa makani;

koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.

19 Mayendedwe a waulesi akunga linga laminga,

koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.

20 Mwana wanzeru akondweretsa atate wake;

koma munthu wopusa apeputsa amake.

21 Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;

koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ake.

22 Zolingalira zizimidwa popanda upo;

koma pochuluka aphungu zikhazikika.

23 Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m’kamwa mwake;

ndi mau a pa nthawi yake kodi sali abwino?

24 Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,

kuti apatuke kusiya kunsi kwa manda.

25 Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;

koma adzalembera mkazi wamasiye malire ake.

26 Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;

koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.

27 Wopindula monyenga avuta nyumba yake;

koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.

28 Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;

koma m’kamwa mwa ochimwa mutsanulira zoipa.

29 Yehova atalikira oipa;

koma pemphero la olungama alimvera.

30 Kuunika kwa maso kukondweretsa mtima;

ndipo pomveka zabwino mafupa amatenga uwisi.

31 Khutu lomvera chidzudzulo cha moyo

lidzakhalabe mwa anzeru.

32 Wokana mwambo apeputsa moyo wake;

koma wosamalira chidzudzulo amatenga nzeru.

33 Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru;

ndipo chifatso chitsogolera ulemu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/15-bf725c31508083cb97a33647d1ef2100.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 16

1 Malongosoledwe a mtima nga munthu;

koma mayankhidwe a lilime achokera kwa Yehova.

2 Njira zonse za munthu ziyera pamaso pake;

koma Yehova ayesa mizimu.

3 Pereka zochita zako kwa Yehova,

ndipo zolingalira zako zidzakhazikika.

4 Zonse Yehova anazipanga zili ndi zifukwa zao;

ngakhale amphulupulu kuti aone tsiku loipa.

5 Yense wonyada mtima anyansa Yehova;

zoonadi sadzapulumuka chilango.

6 Mphulupulu iomboledwa ndi chifundo ndi ntheradi;

apatuka pa zoipa poopa Yehova.

7 Njira za munthu zikakonda Yehova

ayanjanitsana naye ngakhale adani ake.

8 Zapang’ono, pokhala chilungamo,

ziposa phindu lalikulu lopanda chiweruzo.

9 Mtima wa munthu ulingalira njira yake;

koma Yehova ayendetsa mapazi ake.

10 Mau a mlauli ali m’milomo ya mfumu;

m’kamwa mwake simudzachita chetera poweruza.

11 Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova;

ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m’thumba.

12 Kuchita mphulupulu kunyansa mafumu;

pakuti mpando wao wakhazikika ndi chilungamo.

13 Milomo yolungama ikondweretsa mafumu;

wonena zoongoka amkonda.

14 Mkwiyo wa mfumu ndi mithenga ya imfa;

wanzeru adzaukhulula.

15 M’kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo;

kukoma mtima kwake kunga mtambo wa mvula ya masika.

16 Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golide,

kulandira luntha ndi kusankhika koposasiliva?

17 Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa;

wosunga njira yake atchinjiriza moyo wake.

18 Kunyada kutsogolera kuonongeka;

mtima wodzikuza ndi kutsogolera kuphunthwa.

19 Kufatsa mtima ndi osauka

kuposa kugawana zofunkha ndi onyada.

20 Wolabadira mau adzapeza bwino;

ndipo wokhulupirira Yehova adala.

21 Wanzeru mtima adzatchedwa wochenjera;

ndipo kukoma kwa milomo kuonjezera kuphunzira.

22 Nzeru ndi kasupe wa moyo kwa mwini wake;

koma mwambo wa zitsiru ndi utsiru.

23 Mtima wa wanzeru uchenjeza m’kamwa mwake,

nuphunzitsanso milomo yake.

24 Mau okoma ndiwo chisa cha uchi,

otsekemera m’moyo ndi olamitsa mafupa.

25 Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka,

koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.

26 Wantchito adzigwirira yekha ntchito;

pakuti m’kamwa mwake mumfulumiza.

27 Munthu wopanda pake akonzeratu zoipa;

ndipo m’milomo mwake muli moto wopsereza.

28 Munthu wokhota amautsa makani;

kazitape afetsa ubwenzi.

29 Munthu wa chiwawa akopa mnzake,

namuyendetsa m’njira yosakhala bwino.

30 Wotsinzina ndiye aganizira zokhota;

wosunama afikitsa zoipa.

31 Imvi ndiyo korona wa ulemu,

idzapezedwa m’njira ya chilungamo.

32 Wosakwiya msanga aposa wamphamvu;

wolamulira mtima wake naposa wolanda mzinda.

33 Maere aponyedwa pamfunga;

koma ndiye Yehova alongosola zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/16-0ed9dacf531d43cebd0ca0689d79c719.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 17

1 Nyenyeswa youma, pokhala mtendere,

iposa nyumba yodzala nyama yansembe, pali makangano.

2 Kapolo wochita mwanzeru

adzalamulira mwana wochititsa manyazi,

nadzagawana nao abale cholowa.

3 Silivaali ndi mbiya yosungunulira, golide ali ndi ng’anjo;

koma Yehova ayesa mitima.

4 Wochimwa amasamalira milomo yolakwa;

wonama amvera lilime losakaza.

5 Wochitira chiphwete aumphawi atonza Mlengi;

wokondwera ndi tsoka sadzapulumuka chilango.

6 Zidzukulu ndizo korona wa okalamba;

ndipo ulemerero wa ana ndiwo atate ao.

7 Mlomo wangwiro suyenera chitsiru;

ngakhale mlomo wonama suyenera kalonga ndi pang’ono ponse.

8 Wolandira chokometsera mlandu achiyesa ngale;

paliponse popita iye achenjera.

9 Wobisa cholakwa afunitsa chikondano;

koma wobwerezabwereza mau afetsa ubwenzi.

10 Chidzudzulo chilowa m’kati mwa wozindikira,

kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.

11 Woipa amafuna kupanduka kokha;

koma adzamtumizira mthenga wankhanza.

12 Kukomana ndi chitsiru m’kupusa kwake

kuopsa koposa chilombo chochichotsera anake.

13 Wobwezera zabwino zoipa,

zoipa sizidzamchokera kwao.

14 Chiyambi cha ndeu chifanana ndi kutsegulira madzi;

tsono kupikisana kusanayambe tasiya makani.

15 Wokometsa mlandu wa wamphulupulu,

ndi wotsutsa wolungama,

onse awiriwa amnyansa Yehova.

16 Kodi bwanji mtengo wogulira nzeru uli m’dzanja la chitsiru,

popeza wopusa alibe mtima?

17 Bwenzi limakonda nthawi zonse;

ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

18 Munthu wosowa nzeru apangana kulipirira wina,

napereka chikole pamaso pa mnzake.

19 Wokonda ndeu akonda kulakwa;

ndipo wotalikitsa khomo lake afunafuna kuonongeka.

20 Wokhota mtima sadzapeza bwino;

ndipo mwini lilime lokhota adzagwa m’zoipa.

21 Wobala chitsiru adzichititsa chisoni;

ndipo atate wa wopusa sakondwa.

22 Mtima wosekerera uchiritsa bwino;

koma mzimu wosweka uphwetsa mafupa.

23 Munthu woipa alandira chokometsera mlandu chotulutsa m’mfunga,

kuti apatukitse mayendedwe a chiweruzo.

24 Nzeru ili pamaso pa wozindikira;

koma maso a wopusa ali m’malekezero a dziko.

25 Mwana wopusa achititsa atate wake chisoni,

namvetsa zowawa amake wombala.

26 Kulipiritsa wolungama sikuli kwabwino,

ngakhale kukwapula akulu chifukwa aongoka mtima.

27 Wopanda chikamwakamwa apambana kudziwa;

ndipo wofatsa mtima ali wanzeru.

28 Ngakhale chitsiru chikatonthola achiyesa chanzeru;

posunama ali wochenjera.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/17-cea309feb0c02552c48bba5eca7424da.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 18

1 Wopanduka afunafuna chifuniro chake,

nakangana ndi nzeru yonse yeniyeni.

2 Wopusa sakondwera ndi kuzindikira;

koma kungovumbulutsa za m’mtima mwake.

3 Pakudza wamphulupulu padzanso kunyoza;

manyazi natsagana ndi chitonzo.

4 Mau a m’kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya;

kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.

5 Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankho sikuli kwabwino,

ngakhale kuchitira chetera wolungama.

6 Milomo ya wopusa ifikitsa makangano;

ndipo m’kamwa mwake muputa kukwapulidwa.

7 M’kamwa mwa wopusa mumuononga,

milomo yake ikhala msampha wa moyo wake.

8 Mau akazitape akunga zakudya zolongosoka,

zotsikira m’kati mwa mimba.

9 Wogwira ntchito mwaulesi

ndiye mbale wake wa wosakaza.

10 Dzina la Yehova ndilo nsanja yolimba;

wolungama athamangiramo napulumuka.

11 Chuma cha wolemera ndicho mzinda wake wolimba;

alingalira kuti ndicho khoma lalitali.

12 Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;

koma chifatso chitsogolera ulemu.

13 Wobwezera mau asanamvetse apusa,

nadzichititsa manyazi.

14 Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;

koma ndani angatukule mtima wosweka?

15 Mtima wa wozindikira umaphunzira;

khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

16 Mtulo wa munthu umtsegulira njira,

numfikitsa pamaso pa akulu.

17 Woyamba kudzinenera ayang’anika wolungama;

koma mnzake afika namuululitsa zake zonse.

18 Maere aletsa makangano,

nulekanitsa amphamvu.

19 Kupembedza mbale utamchimwira nkovuta,

kulanda mzinda wolimba nkosavuta;

makangano akunga mipiringidzo ya linga.

20 Mimba ya munthu idzakhuta zipatso za m’kamwa mwake;

iye nadzakhuta phindu la milomo yake.

21 Lilime lili ndi mphamvu pa imfa ndi moyo;

wolikonda adzadya zipatso zake.

22 Wopeza mkazi apeza chinthu chabwino;

Yehova amkomera mtima.

23 Wosauka amadandaulira;

koma wolemera ayankha mwaukali.

24 Woyanjana ndi ambiri angodziononga;

koma lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/18-2ffd527be5c96b42d81c856660161173.mp3?version_id=1068—

Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 19

1 Wosauka woyenda mwangwiro

aposa wokhetsa milomo ndi wopusa.

2 Kukhumba kosadziwa sikuli kwabwino;

ndipo wofulumira ndi mapazi ake amachimwa.

3 Utsiru wa munthu ukhotetsa njira yake;

mtima wake udandaula pa Yehova.

4 Chuma chionjezetsa mabwenzi ambiri;

koma mnzake wa waumphawi amleka.

5 Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa;

wolankhula mabodza sadzapulumuka.

6 Ambiri adzapembedza waufulu;

ndipo yense ndi bwenzi la munthu wopatsa.

7 Abale onse a wosauka amuda;

nanga mabwenzi ake kodi satanimphirana naye?

Awatsata ndi mau, koma kuli zii.

8 Wolandira nzeru akonda moyo wake;

wosunga luntha adzapeza zabwino.

9 Mboni yonama sidzapulumuka chilango;

wolankhula mabodza adzaonongeka.

10 Wopusa sayenera kukhala ndi zinthu zolongosoka;

nanga kapolo ayenera kulamulira akalonga kodi?

11 Kulingalira kwa munthu kuchedwetsa mkwiyo;

ulemerero wake uli wakuti akhululukire cholakwa.

12 Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango;

koma kukoma mtima kwake kunga mame pamsipu.

13 Mwana wopusa ndiye tsoka la atate wake;

ndipo makangano a mkazi ndiwo kudonthadonthabe.

14 Nyumba ndi chuma ndizo cholowa cha atate;

koma mkazi wanzeru achokera kwa Yehova.

15 Ulesi ugonetsa tulo tofa nato;

ndipo moyo wamkhongono udzamva njala.

16 Wosunga lamulo asunga moyo wake;

wonyalanyaza mayendedwe ake adzafa.

17 Wochitira waumphawi chifundo abwereka Yehova;

adzambwezera chokoma chakecho.

18 Menya mwanako, chiyembekezero chilipo,

osafunitsa kumuononga.

19 Munthu waukali alipire mwini;

pakuti ukampulumutsa udzateronso.

20 Tamvera uphungu, nulandire mwambo,

kuti ukhale wanzeru pa chimaliziro chako.

21 Muli zolingalira zambiri m’mtima mwa munthu;

koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.

22 Chotikondetsa munthu ndicho kukoma mtima kwake;

ndipo wosauka apambana munthu wonama.

23 Kuopa Yehova kupatsa moyo;

wokhala nako adzakhala wokhuta;

zoipa sizidzamgwera.

24 Waulesi alonga dzanja lake m’mbale,

osalibwezanso kukamwa kwake.

25 Menya wonyoza, ndipo achibwana adzachenjera;

nudzudzule wozindikira adzazindikira nzeru.

26 Wolanda za atate, ndi wopirikitsa amai,

ndiye mwana wochititsa manyazi ndi wogwetsa nkhope.

27 Ukangofuna, mwananga, kusochera kusiya mau akudziwitsa,

leka kumva mwambo.

28 Mboni yopanda pake inyoza chiweruzo;

m’kamwa mwa amphulupulu mumeza zoipa.

29 Akonzera onyoza chiweruzo,

ndi mikwingwirima pamsana pa opusa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/19-c425ba6bdcf12be7ad411a40b3222ef1.mp3?version_id=1068—