Akulu a Ayuda apangana amgwire Yesu
1 Ndipo panali pamene Yesu anatha mau onse amenewa, anati kwaophunziraake,
2 Mudziwa kuti akapita masiku awiri,Paskaafika, ndipoMwana wa Munthuadzaperekedwa kupachikidwa pamtanda.
3 Pomwepo anasonkhana ansembe aakulu, ndi akulu a anthu, kubwalo la mkulu wa ansembe, dzina lake Kayafa;
4 nakhala upo wakuti amgwire Yesu ndi chinyengo, namuphe.
5 Koma ananena iwo, pa nthawi ya chikondwerero iai, kuti pasakhale phokoso la anthu.
Yesu m’nyumba ya Simoni wakhate
6 Ndipo pamene Yesu anali mu Betaniya, m’nyumba ya Simoni wakhate,
7 anadza kwa Iye mkazi, anali nayo nsupa ya alabastero ndi mafuta onunkhira bwino a mtengo wapatali, nawatsanulira pamutu pake, m’mene Iye analikukhala pachakudya.
8 Koma m’mene ophunzira anaona, anada mtima, nanena, Chifukwa ninji kuononga kumeneku?
9 Pakuti mafuta awa akadagulitsa ndalama zambiri, ndi kuzipatsa anthu aumphawi.
10 Koma Yesu podziwa, anati kwa iwo, Mumvutiranji mkaziyu? Popeza andichitira Ine ntchito yabwino.
11 Pakuti nthawi zonse muli nao aumphawi pamodzi nanu; koma simuli ndi Ine nthawi zonse.
12 Pakuti mkaziyo, m’mene anathira mafuta awa pathupi panga, wandichitiratu ichi pa kuikidwa kwanga.
13 Indetu ndinena kwa inu, kumene kulikonse Uthenga uwu Wabwino udzalalikidwa m’dziko lonse lapansi, ichi chimene mkaziyo anachitachi chidzakambidwanso chikumbukiro chake.
Mphotho ya kumpereka Yesu
14 Pomwepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo, dzina lake Yudasi Iskariote, anamuka kwa ansembe aakulu,
15 nati, Mufuna kundipatsa chiyani, ndipo ine ndidzampereka Iye kwa inu? Ndipo iwo anamwerengera iye ndalama zasilivamakumi atatu.
16 Ndipo kuyambira pamenepo iye anafunafuna nthawi yabwino yakuti ampereke Iye.
Paska wotsiriza
17 Ndipo tsiku loyamba la mkate wopanda chotupitsa, ophunzira anadza kwa Yesu, nati, Mufuna tikakonzere kuti Paska, kuti mukadye?
18 Nati Iye, Mukani kumzinda kwa munthu wina wake, mukati kwa Iye, Mphunzitsi anena, Nthawi yanga yayandikira; ndidzadya Paska kwanu pamodzi ndi ophunzira anga.
19 Ndipo ophunzira anachita monga Yesu anawauza, nakonza Paska.
20 Ndipo pakufika madzulo, Iye analinkukhala pachakudya pamodzi ndi ophunzira khumi ndi awiri;
21 ndipo m’mene analinkudya, Iye anati, Indetu ndinena kwa inu, mmodzi wa inu adzandipereka Ine.
22 Ndipo iwo anagwidwa ndi chisoni chachikulu, nayamba kunena kwa Iye mmodzimmodzi, Kodi ndine, Ambuye?
23 Ndipo Iye anayankha nati, Iye amene asunsa pamodzi ndi Ine dzanja lake m’mbale, yemweyu adzandipereka Ine.
24 Mwana wa Munthu achokatu, monga kunalembedwa za Iye; koma tsoka ali nalo munthu amene Mwana wa Munthu aperekedwa ndi iye! Kukadakhala bwino kwa munthuyo ngati sakadabadwa.
25 Ndipo Yudasi, womperekayo anayankha nati, Kodi ndine,Rabi? Iye ananena kwa iye, Iwe watero.
Mgonero wa Ambuye
26 Ndipo pamene iwo analinkudya, Yesu anatenga mkate, nadalitsa, naunyema; ndipo m’mene anapatsa kwa ophunzira, anati, Tengani, idyani; ichi ndi thupi langa.
27 Ndipo pamene anatenga chikho, anayamika, napatsa iwo, nanena, Mumwere ichi inu nonse,
28 pakuti ichi ndi mwazi wanga wa pangano wothiridwa chifukwa cha anthu ambiri ku kuchotsa machimo.
29 Ndipo ndinena kwa inu, sindidzamwanso chipatso ichi champesa, kufikira tsiku limene ndidzamwa chatsopano, pamodzi ndi inu, mu Ufumu wa Atate wanga.
30 Ndipo pamene anaimba nyimbo, anatuluka kunka kuphiri la Azitona.
Yesu achenjeza Petro
31 Pamenepo Yesu ananena kwa iwo, Inu nonse mudzakhumudwa chifukwa cha Ine usiku uno; pakuti kwalembedwa,
Ndidzakantha mbusa,
ndipo zidzabalalika
nkhosa za gulu.
32 Koma nditauka ndidzatsogolera inu ku Galileya.
33 Koma Petro ananena kwa Iye, Ngakhale onse adzakhumudwa chifukwa cha Inu, ine sindidzakhumudwa nthawi zonse.
34 Yesu anati kwa iye, Indetu ndinena kwa iwe, kuti usiku uno, tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.
35 Petro ananena kwa Iye, Ngakhale ine ndikafa ndi Inu, sindidzakukanani Inu iai. Anateronso ophunzira onse.
Yesu mu Getsemani
36 Pomwepo Yesu anadza ndi iwo kumalo otchedwa Getsemani, nanena kwa ophunzira ake, Bakhalani inu pompano, ndipite uko ndikapemphere.
37 Ndipo anatenga Petro ndi ana awiri a Zebedeo pamodzi naye, nayamba kugwidwa ndi chisoni ndi kuthedwa nzeru.
38 Pamenepo ananena kwa iwo, Moyo wanga uli wozingidwa ndi chisoni cha kufika nacho kuimfa; khalani pano muchezere pamodzi ndi Ine.
39 Ndipo anamuka patsogolo pang’ono, nagwa nkhope yake pansi, napemphera, nati, Atate ngati nkutheka, chikho ichi chindipitirire Ine; koma si monga ndifuna Ine, koma Inu.
40 Ndipo anadza kwa ophunzira, nawapeza iwo ali m’tulo, nanena kwa Petro, Nkutero kodi? Simungathe kuchezera ndi Ine mphindi imodzi?
41 Chezerani ndi kupemphera, kuti mungalowe m’kuyesedwa: mzimutu uli wakufuna, koma thupi lili lolefuka.
42 Anamukanso kachiwiri, napemphera, nati, Atate wanga, ngati ichi sichingandipitirire, koma ndimwere ichi, kufuna kwanu kuchitidwe.
43 Ndipo anabweranso, nawapeza iwo ali m’tulo, pakuti zikope zao zinalemera ndi tulo.
44 Ndipo anawasiyanso, napemphera kachitatu, nateronso mau omwewo.
45 Pomwepo anadza kwa ophunzira, nanena kwa iwo, Gonani nthawi yatsalayi, mupumule; onani, nthawi yafika, ndipo Mwana wa Munthu aperekedwa m’manja a ochimwa.
46 Ukani, timuke; taonani, iye wakundipereka wayandikira.
Amgwira Yesu
47 Ndipo Iye ali chilankhulire, onani, Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anadza, ndi pamodzi ndi iye khamu lalikulu la anthu, ndi malupanga ndi mikunkhu, kuchokera kwa ansembe aakulu ndi akulu a anthu.
48 Koma wompereka Iye anawapatsa chizindikiro, nanena, Iye amene ndidzampsompsona ndiyeyo, mumgwire Iye.
49 Ndipo pomwepo anadza kwa Yesu, nati, Tikuoneni, Rabi; nampsompsonetsa.
50 Ndipo Yesu anati kwa iye, Mnzanga, wafikiranji iwe? Pomwepo iwo anadza, namthira Yesu manja, namgwira Iye.
51 Ndipo onani, mmodzi wa iwo anali pamodzi ndi Yesu, anatansa dzanja lake, nasolola lupanga lake, nakantha kapolo wa mkulu wa ansembe, nadula khutu lake.
52 Pomwepo Yesu ananena kwa iye, Tabweza lupanga lako m’chimakemo, pakuti onse akugwira lupanga adzaonongeka ndi lupanga.
53 Kapena uganiza kuti sindingathe kupemphera Atate wanga, ndipo Iye adzanditumizira tsopano lino mabungwe aangelooposa khumi ndi awiri?
54 Koma pakutero malembo adzakwaniridwa bwanji, pakuti kuyenera chomwecho?
55 Nthawi yomweyo Yesu anati kwa makamuwo a anthu, Kodi munatulukira kundigwira Ine ndi malupanga ndi mikunkhu, ngati wachifwamba? Tsiku ndi tsiku ndimakhala mu Kachisi kuphunzitsa, ndipo simunandigwire.
56 Koma izi zonse zinachitidwa, kuti zolembedwa za aneneri zikwaniridwe. Pomwepo ophunzira onse anamsiya Iye, nathawa.
Yesu kubwalo la akulu a Ayuda
57 Ndipo iwo akugwira Yesu ananka naye kwa Kayafa, mkulu wa ansembe, kumene adasonkhana alembi ndi akulu omwe.
58 Koma Petro anamtsata kutali, kufikira kubwalo la mkulu wa ansembe, nalowamo, nakhala pansi ndi anyamata, kuti aone chimaliziro.
59 Ndipo ansembe aakulu ndi akulu a milandu onse anafunafuna umboni wonama wakutsutsa Yesu, kuti amuphe Iye;
60 koma sanaupeze zingakhale mboni zonama zambiri zinadza. Koma pambuyo pake anadza awiri,
61 nati, Uyu ananena kuti, Ndikhoza kupasula Kachisi wa Mulunguyu, ndi kummanganso masiku atatu.
62 Ndipo mkulu wa ansembe anaimirira, nati kwa Iye, Suvomera kanthu kodi? Nchiyani ichi chimene awa akunenera Iwe?
63 Koma Yesu anangokhala chete. Ndipo mkulu wa ansembe ananena kwa Iye, Ndikulumbiritsa Iwe pa Mulungu wamoyo, kuti utiuze ife ngati Iwe ndiweKhristu, Mwana wa Mulungu.
64 Yesu anati kwa iye, Mwatero, koma ndinenanso kwa inu, Kuyambira tsopano mudzaona Mwana wa Munthu ali kukhala kudzanja lamanja la mphamvu, ndi kufika pa mitambo ya kumwamba.
65 Pomwepo mkulu wa ansembe anang’amba zovala zake, nati, Achitira Mulungu mwano; tifuniranji mboni zina? Onani, tsopano mwamva mwanowo;
66 muganiza bwanji? Iwo anayankha nati, Ali woyenera kumupha.
67 Pomwepo iwo anathira malovu pankhope pake, nambwanyula Iye; ndipo ena anampanda khofu,
68 nati, Utilote ife, Khristu Iwe; wakumenya Iwe ndani?
Petro akana Yesu
69 Ndipo Petro adakhala pabwalo: ndipo mdzakazi anadza kwa iye, nanena, Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.
70 Koma iye anakana pamaso pa anthu onse, kuti, Chimene unena sindichidziwa.
71 Ndipo pamene iye anatuluka kunka kuchipata, mkazi wina anamuona, nati kwa iwo a pomwepo, Uyonso anali ndi Yesu Mnazarayo.
72 Ndipo anakananso ndi chilumbiro, kuti, Sindidziwa munthuyo.
73 Ndipo popita nthawi yaing’ono, iwo akuimapo anadza, nati kwa Petro, Zoonadi, iwenso uli wa iwo; pakuti malankhulidwe ako akuzindikiritsa iwe.
74 Pamenepo iye anayamba kutemberera ndi kulumbira, kuti, Sindidziwa munthuyo. Ndipo pompo tambala analira.
75 Ndipo Petro anakumbukira mau amene Yesu adati, Asanalire tambala udzandikana katatu. Ndipo anatulukira kunja, nalira ndi kuwawa mtima.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MAT/26-c3f0823e2303af0b9882362048008b5e.mp3?version_id=1068—