Categories
MASALIMO

MASALIMO 70

Davide apempha Mulungu amlanditse msanga

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide, la chikumbutso.

1 Fulumirani kundipulumutsa, Mulungu!

Fulumirani kundithandiza, Yehova.

2 Achite manyazi, nadodome

amene afuna moyo wanga.

Abwezedwe m’mbuyo, napepulidwe

amene akonda kundichitira choipa.

3 Abwerere, kukhale mphotho ya manyazi ao

amene akuti, Hede, hede.

4 Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu;

nanene kosalekeza iwo akukonda chipulumutso chanu,

abuke Mulungu.

5 Koma ine ndine wozunzika ndi waumphawi;

mundifulumirire, Mulungu.

Inu ndinu mthandizi wanga ndi Mpulumutsi wanga;

musachedwe, Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/70-251047a461c8e820f60f8ead5989c355.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 71

Nkhalamba idzaponya kwa Mulungu amene anamkhulupirira kuyambira ubwana wake

1 Ndikhulupirira Inu, Yehova.

Ndisachite manyazi nthawi zonse.

2 Ndikwatuleni m’chilungamo chanu, ndi kundilanditsa,

nditcherereni khutu lanu ndi kundipulumutsa.

3 Mundikhalire thanthwe lokhalamo, lopitako kosaleka;

mwalamulira kundipulumutsa;

popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.

4 Ndilanditseni, Mulungu wanga, m’dzanja la woipa,

m’dzanja la munthu wosalungama ndi wachiwawa.

5 Pakuti Inu ndinu chiyembekezo changa, Ambuye Yehova;

mwandikhalira wokhulupirika kuyambira ubwana wanga.

6 Inu munandigwiriziza kuyambira ndisanabadwe,

kuyambira pa thupi la mai wanga wondichitira zokoma ndinu;

ndidzakulemekezani kosalekeza.

7 Ndikhala chodabwitsa kwa ambiri;

koma Inu ndinu pothawira panga polimba.

8 M’kamwa mwanga mudzadzala lemekezo lanu,

ndi ulemu wanu tsiku lonse.

9 Musanditaye mu ukalamba wanga;

musandisiye, pakutha mphamvu yanga.

10 Pakuti adani anga alankhula za ine;

ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,

11 ndi kuti, Wamsiya Mulungu.

Mlondoleni, mgwireni; popeza palibe wompulumutsa.

12 Musandikhalire kutali, Mulungu;

fulumirani kundithandiza, Mulungu.

13 Adani a moyo wanga achite manyazi, nathawe;

chotonza ndi chimpepulo zikute ondifunira choipa.

14 Koma ine ndidzayembekeza kosaleka,

ndipo ndidzaonjeza kukulemekezani.

15 Pakamwa panga padzafotokozera chilungamo chanu,

ndi chipulumutso chanu tsiku lonse;

pakuti sindidziwa mawerengedwe ake.

16 Ndidzamuka mu mphamvu ya Ambuye Yehova;

ndidzatchula chilungamo chanu, inde chanu chokha.

17 Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira ubwana wanga;

ndipo kufikira lero ndilalikira zodabwitsa zanu.

18 Poteronso pokalamba ine ndi kukhala nazo imvi musandisiye, Mulungu;

kufikira nditalalikira mbadwo uwu za dzanja lanu,

mphamvu yanu kwa onse akudza m’mbuyo.

19 Chilungamo chanunso, Mulungu, chifikira kuthambo;

Inu amene munachita zazikulu,

akunga Inu ndani, Mulungu?

20 Inu, amene munationetsa nsautso zambiri ndi zoipa,

mudzatipatsanso moyo,

ndi kutitenganso munsi mwa dziko.

21 Mundionjezere ukulu wanga,

ndipo munditembenukire kundisangalatsa.

22 Ndiponso ndidzakuyamikani ndi chisakasa,

kubukitsa choonadi chanu, Mulungu wanga;

ndidzakuimbirani nyimbo ndi zeze,

ndinu Woyerayo wa Israele.

23 Milomo yanga idzafuula mokondwera poimbira Inu nyimbo;

inde, moyo wanga umene munaombola.

24 Lilime langa lomwe lidzalankhula za chilungamo chanu tsiku lonse,

pakuti ofuna kundichitira choipa achita manyazi, nadodoma.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/71-0771d2c3ef063cd4dd268f590b828ffa.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 72

Za ufumu wa Mfumu yokoma

Salimo la Solomoni.

1 Patsani mfumu maweruzo anu, Mulungu,

ndi mwana wa mfumu chilungamo chanu.

2 Potero adzanenera anthu anu mlandu ndi m’chilungamo,

ndi ozunzika anu ndi m’chiweruzo.

3 Mapiri adzatengera anthu mtendere,

timapiri tomwe, m’chilungamo.

4 Adzaweruza ozunzika a mwa anthu,

adzapulumutsa ana aumphawi,

nadzaphwanya wosautsa.

5 Adzakuopani momwe likhalira dzuwa ndi mwezi,

kufikira mibadwomibadwo.

6 Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga,

monga mvula yothirira dziko.

7 Masiku ake wolungama adzakhazikika;

ndi mtendere wochuluka, kufikira sipadzakhala mwezi.

8 Ndipo adzachita ufumu kuchokera kunyanja kufikira kunyanja,

ndi kuchokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.

9 Okhala m’chipululu adzagwadira pamaso pake;

ndi adani ake adzaluma nthaka.

10 Mafumu a ku Tarisisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera nacho chopereka;

mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso.

11 Inde mafumu onse adzamgwadira iye,

amitunduonse adzamtumikira.

12 Pakuti adzapulumutsa waumphawi wofuulayo;

ndi wozunzika amene alibe mthandizi.

13 Adzachitira nsoni wosauka ndi waumphawi,

nadzapulumutsa moyo wa aumphawi.

14 Adzaombola moyo wao ku chinyengo ndi chiwawa;

ndipo mwazi wao udzakhala wa mtengo pamaso pake.

15 Ndipo iye adzakhala ndi moyo;

ndipo adzampatsa golide wa ku Sheba;

nadzampempherera kosalekeza;

adzamlemekeza tsiku lonse.

16 M’dzikomo mudzakhala dzinthu dzochuluka

pamwamba pa mapiri;

zipatso zake zidzati waa, ngati za ku Lebanoni,

ndipo iwo a m’mizinda adzaphuka ngati msipu wapansi.

17 Dzina lake lidzakhala kosatha,

momwe likhalira dzuwa dzina lake lidzamvekera zidzukulu.

Ndipo anthu adzadalitsidwa mwa Iye;

amitundu onse adzamutcha wodala.

18 Wolemekezeka Yehova Mulungu, Mulungu wa Israele,

amene achita zodabwitsa yekhayo.

19 Ndipo dzina lake la ulemerero lidalitsike kosatha;

ndipo dziko lonse lapansi lidzale nao ulemerero wake.

Amen, ndi Amen.

20 Mapemphero a Davide mwana wa Yese atha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/72-afe1e9589ee32599b3e095cbb851cd4d.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 73

Kupindula kwa oipa kumakayikitsa pa chilungamo cha Mulungu, koma chitsiriziro chao chitivomerezetsa chilungamocho

Salimo la Asafu.

1 Indedi Mulungu achitira Israele zabwino,

iwo a mtima wa mbee.

2 Koma ine, ndikadagwa;

mapazi anga akadaterereka.

3 Pakuti ndinachitira nsanje odzitamandira,

pakuona mtendere wa oipa.

4 Pakuti palibe zomangira pakufa iwo,

ndi mphamvu yao njolimba.

5 Savutika monga anthu ena;

sasautsika monga anthu ena.

6 Chifukwa chake kudzikuza kunga unyolo pakhosi pao;

achivala chiwawa ngati malaya.

7 Kunenepa kwao kutuzulitsa maso ao,

malingaliro a mitima yao asefukira.

8 Achita zaphwete nalankhula moipa za kusautsa,

alankhula modzitama.

9 Pakamwa pao anena zam’mwamba,

ndipo lilime lao liyendayenda m’dziko lapansi.

10 Chifukwa chake anthu ake amabwera kudza kuno,

ndipo chikho chodzala ndi madzi achigugudiza.

11 Namati, Akachidziwa bwanji Mulungu?

Kodi Wam’mwambamwamba ali nayo nzeru?

12 Tapenyani, oipa ndi awa;

ndipo pokhazikika chikhazikikire aonjezerapo pa chuma chao.

13 Indedi, ndinayeretsa mtima wanga kwachabe,

ndipo ndinasamba m’manja mosalakwa.

14 Popeza andisautsa tsiku lonse,

nandilanga mamawa monse,

15 ndikadati, Ndidzafotokozera chotere,

taonani, ndikadachita chosakhulupirika ndi mbadwo wa ana ako.

16 Pamene ndinayesa kudziwitsa ichi,

ndinavutika nacho;

17 mpaka ndinalowa m’zoyera za Mulungu,

ndi kulingalira chitsiriziro chao.

18 Indedi muwaika poterera,

muwagwetsa kuti muwaononge.

19 Ha? M’kamphindi ayesedwa bwinja;

athedwa konse ndi zoopsa.

20 Monga anthu atauka, apepula loto;

momwemo, Inu Ambuye, pakuuka

mudzapeputsa chithunzithunzi chao.

21 Pakuti mtima wanga udawawa,

ndipo ndinalaswa mu impso zanga;

22 ndinali wam’thengo, wosadziwa kanthu;

ndinali ngati nyama pamaso panu.

23 Koma ndikhala ndi Inu chikhalire,

mwandigwira dzanja langa la manja.

24 Mudzanditsogolera ndi uphungu wanu,

ndipo mutatero, mudzandilandira mu ulemerero.

25 Ndili ndi yani Kumwamba, koma Inu?

Ndipo padziko lapansi palibe wina wondikonda koma Inu.

26 Likatha thupi langa ndi mtima wanga,

Mulungu ndiye thanthwe la mtima wanga,

ndi cholandira changa chosatha.

27 Pakuti, taonani, iwo okhala patali ndi Inu adzaonongeka;

muononga onse akupembedza kwina, kosiyana ndi Inu.

28 Koma ine, kundikomera kuyandikiza kwa Mulungu.

Ndimuyesa Ambuye Yehova pothawirapo ine,

kuti ndifotokozere ntchito zanu zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/73-83b70a1219340538ba838677699ab073.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 74

Malo oyera adetsedwa. Apempha Mulungu akumbuke chipangano chao

Chilangizo cha Asafu.

1 Mulungu, munatitayiranji chitayire?

Mkwiyo wanu ufukiranji pa nkhosa za kubusa kwanu?

2 Kumbukirani msonkhano wanu, umene munaugula kale,

umene munauombola ukhale fuko la cholowa chanu;

Phiri laZiyonilimene mukhalamo.

3 Nyamulani mapazi anu kukapenya mapasukidwe osatha,

zoipa zonse adazichita mdani m’malo opatulika.

4 Otsutsana ndi Inu abangula pakati pa msonkhano wanu;

aika mbendera zao zikhale zizindikiro.

5 Anaoneka ngati osamula nkhwangwa kunkhalango.

6 Ndipo tsopano aphwanya zosemeka zake zonse

ndi nkhwangwa ndi nyundo.

7 Anatentha malo anu opatulika;

anaipsa ndi kugwetsa pansi mokhalamo dzina lanu.

8 Ananena mumtima mwao, Tiwapasule pamodzi;

anatentha zosonkhaniramo za Mulungu zonse, m’dzikomo.

9 Sitiziona zizindikiro zathu;

palibensomneneri;

ndipo mwa ife palibe wina wakudziwa mpaka liti.

10 Wotsutsanayo adzatonza kufikira liti, Mulungu?

Kodi mdani adzanyoza dzina lanu nthawi yonse?

11 Mubwezeranji dzanja lanu, ndilo dzanja lamanja lanu?

Mulitulutse kuchifuwa chanu ndipo muwatheretu.

12 Koma Mulungu ndiye mfumu yanga kuyambira kale,

wochita zakupulumutsa pakati padziko lapansi.

13 Mudagawa nyanja ndi mphamvu yanu;

mudaswa mitu ya zoopsa za m’madzi.

14 Mudaphwanya mitu yaLeviyatani;

mudampereka akhale chakudya cha zilombo za m’chipululu.

15 Mudagawa kasupe ndi mtsinje;

mudaphwetsa mitsinje yaikulu.

16 Usana ndi wanu, usikunso ndi wanu,

munakonza kuunika ndi dzuwa.

17 Munaika malekezero onse a dziko lapansi;

munalenga dzinja ndi malimwe.

18 Mukumbukire ichi, Yehova, mdaniyo anatonza,

ndipo anthu opusa ananyoza dzina lanu.

19 Musapereke moyo wa njiwa yanu kwa chilombo;

musamaiwala moyo wa ozunzika anu nthawi yonse.

20 Samalirani chipanganocho;

pakuti malo a mdima a m’dziko adzala ndi zokhalamo chiwawa.

21 Okhalira mphanthi asabwere nao manyazi;

wozunzika ndi waumphawi alemekeze dzina lanu.

22 Nyamukani, Mulungu, mudzinenere mlandu nokha;

kumbukirani momwe akutonzani wopusa tsiku lonse.

23 Musaiwale mau a iwo otsutsana ndi Inu;

kusokosera kwa iwo akuukirani Inu kumakwera kosaleka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/74-f6b2ca6dd029419aab82d250c90fd897.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 75

Mulungu woweruza asiyanitsa pakati pa odzikuza ndi olungama

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Altasyeti. Salimo la Asafu. Nyimbo.

1 Tikuyamikani Inu, Mulungu;

tiyamika, pakuti dzina lanu lili pafupi;

afotokozera zodabwitsa zanu.

2 Pakuona nyengo yake ndidzaweruza molunjika.

3 Lasungunuka dziko lapansi, ndi onse okhalamo;

ndinachirika mizati yake.

4 Ndinati kwa odzitamandira,

musamachita zodzitamandira;

ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga;

5 musamakwezetsa nyanga yanu;

musamalankhula ndi khosi louma.

6 Pakuti kukuzaku sikuchokera kum’mawa,

kapena kumadzulo, kapena kuchipululu.

7 Pakuti Mulungu ndiye woweruza;

achepsa wina, nakuza wina.

8 Pakuti m’dzanja la Yehova muli chikho;

ndi vinyo wake achita thovu;

chidzala ndi zosakanizira, ndipo atsanulako.

Indedi, oipa onse a padziko lapansi adzamwa

nadzagugudiza nsenga zake.

9 Koma ine ndidzalalikira kosalekeza,

ndidzaimbira zomlemekeza Mulungu wa Yakobo.

10 Ndipo ndidzatseteka nyanga zonse za oipa;

koma nyanga za wolungama zidzakwezeka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/75-52b7b03dd59f18d15cd25d480b6410d9.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 76

Ulemerero ndi mphamvu ya Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Salimo la Asafu. Nyimbo.

1 Mulungu adziwika mwa Yuda,

dzina lake limveka mwa Israele.

2 Msasa wake unali mu Salemu,

ndipo pokhala Iye muZiyoni.

3 Pomwepo anathyola mivi ya pauta;

chikopa, ndi lupanga, ndi nkhondo.

4 Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka

wakuposa mapiri muli achifwamba.

5 Olimba mtima chifunkhidwa chuma chao, agona tulo tao;

amuna onse amphamvu asowa manja ao.

6 Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo,

galeta ndi kavalo yemwe anagwa m’tulo.

7 Inu ndinu woopsa;

ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala chilili ndani pamaso panu?

8 Mudamveketsa chiweruzo chochokera Kumwamba;

dziko lapansi linachita mantha, nilinakhala chete,

9 pakuuka Mulungu kuti aweruze,

kuti apulumutse ofatsa onse a padziko lapansi.

10 Indedi, kuzaza kwake kwa munthu kudzakulemekezani;

chotsalira cha kuzazaku mudzachiletsa.

11 Windani ndipo chitirani Yehova Mulungu wanu zowindazo;

onse akumzinga abwere nacho chopereka

cha kwa Iye amene ayenera kumuopa.

12 Iye adzadula mzimu wa akulu;

akhala woopsa kwa mafumu a padziko lapansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/76-6d49cd8d3a95a8d09509157e28fcb6e7.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 77

Achita nkhawa pokumbuka zochita Mulungu, koma alimbika mtima pokumbuka zina adazichita Iye

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Yedutuni. Salimo la Asafu.

1 Ndidzafuulira kwa Mulungu ndi mau anga;

kwa Mulungu ndi mau anga, ndipo adzanditcherezera khutu.

2 Tsiku la nsautso yanga ndinafuna Ambuye.

Dzanja langa linatambalika usiku, losaleka;

mtima wanga unakana kutonthozedwa.

3 Ndikumbukira Mulungu ndipo ndivutika;

ndilingalira ndipo mzimu wanga ukomoka.

4 Mundikhalitsa maso;

ndigwidwa mtima wosanena kanthu.

5 Ndinaganizira masiku akale,

zaka zakalekale.

6 Ndikumbukira nyimbo yanga usiku;

ndilingalira mumtima mwanga;

mzimu wanga unasanthula.

7 Kodi Ambuye adzataya nthawi yonse?

Osabwerezanso kukondwera nafe.

8 Chifundo chake chalekeka konsekonse kodi?

Lonjezano lake lidatha kodi ku mibadwo yonse?

9 Kodi Mulungu waiwala kuchita chifundo?

Watsekereza kodi nsoni zokoma zake mumkwiyo?

10 Ndipo ndinati, Chindiwawa ichi;

koma ndikumbukira zaka za dzanja lamanja la Wam’mwambamwamba.

11 Ndidzakumbukira zimene adazichita Yehova;

inde, ndidzakumbukira zodabwitsa zanu zoyambira kale.

12 Ndipo ndidzalingalira ntchito yanu yonse,

ndi kulingalirabe zimene munazichita Inu.

13 Mulungu, m’malo opatulika muli njira yanu;

Mulungu wamkulu ndani monga Mulungu?

14 Inu ndinu Mulungu wakuchita chodabwitsa;

munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.

15 Munaombola anthu anu ndi mkono wanu,

ndiwo ana a Yakobo, ndi a Yosefe.

16 Madziwo anakuonani Mulungu;

anakuonani madziwo; anachita mantha,

zozama zomwe zinanjenjemera.

17 Makongwa anatsanula madzi;

thambo lidamvetsa liu lake;

mivi yanu yomwe inatulukira.

18 Liu la bingu lanu linatengezanatengezana;

mphezi zinaunikira ponse pali anthu;

dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

19 Njira yanu inali m’nyanja,

koyenda Inu nkumadzi aakulu,

ndipo mapazi anu sanadziwike.

20 Munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa,

ndi dzanja la Mose ndi Aroni.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/77-d06cca7a2d01417e2d34d1e031c85145.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 78

Chikondi ndi chipiriro cha Mulungu cha pa Aisraele osakhulupirika

Chilangizo cha Asafu.

1 Tamverani, anthu anga, chilamulo changa;

tcherezani khutu lanu mau a pakamwa panga.

2 Ndidzatsegula pakamwa panga mofanizira;

ndidzatchula zinsinsi zoyambira kale.

3 Zimene tinazimva, ndi kuzidziwa,

ndipo makolo athu anatifotokozera.

4 Sitidzazibisira ana ao,

koma kufotokozera mbadwo ukudzawo zolemekeza za Yehova,

ndi mphamvu yake, ndi zodabwitsa zake zimene anazichita.

5 Anakhazika mboni mwa Yakobo,

naika chilamulo mwa Israele,

ndizo analamulira atate athu,

akazidziwitse ana ao;

6 kuti mbadwo ukudzawo udziwe,

ndiwo ana amene akadzabadwa;

amene adzaimirira nadzafotokozera ana ao.

7 Ndi kuti chiyembekezo chao chikhale kwa Mulungu,

osaiwala zochita Mulungu,

koma kusunga malamulo ake ndiko.

8 Ndi kuti asange makolo ao,

ndiwo mbadwo woukirana ndi wopikisana ndi Mulungu;

mbadwo wosakonza mtima wao,

ndi mzimu wao sunakhazikike ndi Mulungu.

9 Ana a Efuremu okhala nazo zida, oponya nao mauta,

anabwerera m’mbuyo tsiku la nkhondo.

10 Sanasungachipanganocha Mulungu,

nakana kuyenda m’chilamulo chake.

11 Ndipo anaiwala zochita Iye,

ndi zodabwitsa zake zimene anawaonetsa.

12 Anachita chodabwitsa pamaso pa makolo ao,

m’dziko la Ejipito kuchidikha cha Zowani.

13 Anagawa nyanja nawapititsapo;

naimitsa madziwo ngati khoma.

14 Ndipo msana anawatsogolera ndi mtambo

ndi usiku wonse ndi kuunika kwa moto.

15 Anang’alula thanthwe m’chipululu,

ndipo anawamwetsa kochuluka monga m’madzi ozama.

16 Anatulukitsa mitsinje m’thanthwe,

inde anatsikitsa madzi ngati mitsinje.

17 Koma anaonjeza kumchimwira Iye,

kupikisana ndi Wam’mwambamwamba m’chipululu.

18 Ndipo anayesa Mulungu mumtima mwao

ndi kupempha chakudya monga mwa kulakalaka kwao.

19 Ndipo analankhula motsutsana ndi Mulungu;

anati, Kodi Mulungu akhoza kutikonzera podyera m’chipululu?

20 Taonani, anapanda thanthwe, ndi madzi anayendako

ndi mitsinje inasefuka;

kodi adzakhozanso kupatsa mkate?

Kodi adzafunira anthu ake nyama?

21 Chifukwa chake Yehova anamva, nakwiya;

ndipo anayatsa moto pa Yakobo,

ndiponso mkwiyo unakwera pa Israele.

22 Popeza sanakhulupirire Mulungu,

osatama chipulumutso chake.

23 Koma analamulira mitambo ili m’mwamba,

natsegula m’makomo a kumwamba.

24 Ndipo anawavumbitsiramana, adye,

nawapatsa tirigu wa kumwamba.

25 Yense anadya mkate wa angelo,

anawatumizira chakudya chofikira.

26 Anaombetsa m’mwamba mphepo ya kum’mawa,

natsogoza mwera ndi mphamvu yake.

27 Ndipo anawavumbitsira nyama ngati fumbi,

ndi mbalame zouluka ngati mchenga wa kunyanja.

28 Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,

pozungulira pokhala iwo.

29 Potero anadya nakhuta kwambiri;

ndipo anawapatsa chokhumba iwo.

30 Asanathe nacho chokhumba chao,

chakudya chao chili m’kamwa mwao,

31 pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,

ndipo anapha mwa onenepa ao,

nagwetsa osankhika a Israele.

32 Chingakhale ichi chonse anachimwanso,

osavomereza zodabwitsa zake.

33 Potero anathera masiku ao ndi zopanda pake,

ndi zaka zao mwa mantha.

34 Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;

nabwerera, nafunitsitsa Mulungu.

35 Ndipo anakumbukira kuti Mulungu ndiye thanthwe lao,

ndi Mulungu Wam’mwambamwamba Mombolo wao.

36 Koma anamsyasyalika pakamwa pao,

namnamiza ndi lilime lao.

37 Popeza mtima wao sunakonzekere Iye,

ndipo sanakhazikike m’chipangano chake.

38 Koma Iye pokhala ngwa chifundo,

anakhululukira choipa, osawaononga;

nabweza mkwiyo wake kawirikawiri,

sanautse ukali wake wonse.

39 Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu;

mphepo yopita yosabweranso.

40 Kawirikawiri nanga anapikisana ndi Iye kuchigwako,

nammvetsa chisoni m’chipululu.

41 Pakuti anabwerera m’mbuyo, nayesa Mulungu,

nachepsa Woyerayo wa Israele.

42 Sanakumbukire dzanja lake,

tsikuli anawaombola kwa msautsi.

43 Amene anaika zizindikiro zake mu Ejipito,

ndi zodabwitsa zake kuchidikha cha Zowani.

44 Nasanduliza nyanja yao mwazi,

ndi mitsinje yao, kuti sangakhoze kumwa.

45 Anawatumizira pakati pao mitambo ya ntchentche zakuwatha;

ndi achule akuwaononga.

46 Ndipo anapatsa mphuchi dzinthu dzao,

ndi dzombe ntchito yao.

47 Anapha mphesa zao ndi matalala,

ndi mikuyu yao ndi chisanu.

48 Naperekanso zoweta zao kwa matalala,

ndi ng’ombe zao kwa mphezi.

49 Anawatumizira mkwiyo wake wotentha,

kuzaza, ndi kupsa mtima, ndi nsautso,

ndizo gulu la amithenga ochita zoipa.

50 Analambulira mkwiyo wake njira;

sanalekerere moyo wao usafe,

koma anapereka moyo wao kumliri.

51 Ndipo anapha ana oyamba onse a mu Ejipito,

ndiwo oyamba a mphamvu yao m’mahema a Hamu.

52 Koma anatulutsa anthu ake ngati nkhosa,

nawatsogoza ngati gulu la zoweta m’chipululu.

53 Ndipo anawatsogolera mokhulupirika,

kotero kuti sanaope;

koma nyanja inamiza adani ao.

54 Ndipo anawafikitsa kumalire a malo ake oyera,

kuphiri ili, dzanja lamanja lake lidaligula.

55 Ndipo anapirikitsaamitundupamaso pao,

nawagawira cholowa chao, ndi muyeso,

nakhalitsa mafuko a Israele m’mahema mwao.

56 Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam’mwambamwamba,

osasunga mboni zake;

57 koma anabwerera m’mbuyo,

nachita zosakhulupirika monga makolo ao,

anapatuka ngati uta wolenda.

58 Ndipo anautsa mtima wake ndi malo amsanje ao,

namchititsa nsanje ndi mafano osema.

59 Pakumva ichi Mulungu, anakwiya,

nanyozatu Israele;

60 ndipo anachokera chokhalamo cha ku Silo,

chihemacho adachimanga mwa anthu;

61 napereka mphamvu yake mu ukapolo,

ndi ulemerero wake m’dzanja la msautsi.

62 Naperekanso anthu ake kwa lupanga;

nakwiya nacho cholowa chake.

63 Moto unapsereza anyamata ao;

ndi anamwali ao sanalemekezeke.

64 Ansembe ao anagwa ndi lupanga;

ndipo amasiye ao sanachite maliro.

65 Pamenepo Ambuye anauka ngati wam’tulo;

ngati chiphona chakuchita nthungululu ndi vinyo.

66 Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo;

nawapereka akhale otonzeka kosatha.

67 Tero anakana hema wa Yosefe;

ndipo sanasankhe fuko la Efuremu;

68 koma anasankha fuko la Yuda,

Phiri laZiyonilimene analikonda.

69 Ndipo anamanga malo oyera ake ngati kaphiri,

monga dziko lapansi limene analikhazikitsa kosatha.

70 Ndipo anasankha Davide mtumiki wake,

namtenga kumakola a nkhosa.

71 Anamtenga kuja anatsata zoyamwitsa,

awete Yakobo, anthu ake, ndi Israele, cholowa chake.

72 Potero anawaweta monga mwa mtima wake wangwiro;

nawatsogolera ndi luso la manja ake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/78-e2156f04bd933a25a0454c3bfa7e9aca.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 79

Yerusalemu apasuka, apempha Mulungu awathandize

Salimo la Asafu.

1 Mulungu, akunja alowa m’cholowa chanu;

anaipsa Kachisi wanu woyera;

anachititsaYerusalemubwinja.

2 Anapereka mitembo ya atumiki anu ikhale

chakudya cha mbalame za mlengalenga,

nyama ya okondedwa anu anaipereka kwa zilombo za m’dziko.

3 Anakhetsa mwazi wao ngati madzi pozungulira Yerusalemu;

ndipo panalibe wakuwaika.

4 Takhala chotonza cha anansi athu,

ndi choseketsa ndi cholalatitsa iwo akutizinga.

5 Yehova, mudzakwiya nthawi zonse kufikira liti?

Nidzatentha nsanje yanu ngati moto?

6 Thirirani mkwiyo wanu pa akunja osadziwa Inu,

ndi pa maufumu osaitana pa dzina lanu.

7 Pakuti anathera Yakobo,

napasula pokhalira iye.

8 Musakumbukire motitsutsa mphulupulu za makolo athu;

nsoni zokoma zanu zitipeze msanga,

pakuti tafooka kwambiri.

9 Tithandizeni Mulungu wa chipulumutso chathu,

chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu;

ndipo tilanditseni, ndi kutifafanizira zoipa zathu,

chifukwa cha dzina lanu.

10 Anenerenjiamitundu, Ali kuti Mulungu wao?

Kubwezera chilango cha mwazi wa atumiki anu umene anaukhetsa

kudziwike pakati pa amitundu pamaso pathu.

11 Kubuula kwa wandende kufike kuli Inu;

monga mwa mphamvu yanu yaikulu lolani ana a imfa atsale.

12 Ndipo anansi athu amene anatonza Inu

muwabwezere chotonza chao,

kasanu ndi kawiri kumtima kwao, Ambuye.

13 Potero ife anthu anu ndi nkhosa zapabusa panu

tidzakuyamikani kosatha;

tidzafotokozera chilemekezo chanu ku mibadwomibadwo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/79-e2d05ecb3a115be44ba2d6c2838e09ec.mp3?version_id=1068—