Chikondi ndi chipiriro cha Mulungu cha pa Aisraele osakhulupirika
Chilangizo cha Asafu.
1 Tamverani, anthu anga, chilamulo changa;
tcherezani khutu lanu mau a pakamwa panga.
2 Ndidzatsegula pakamwa panga mofanizira;
ndidzatchula zinsinsi zoyambira kale.
3 Zimene tinazimva, ndi kuzidziwa,
ndipo makolo athu anatifotokozera.
4 Sitidzazibisira ana ao,
koma kufotokozera mbadwo ukudzawo zolemekeza za Yehova,
ndi mphamvu yake, ndi zodabwitsa zake zimene anazichita.
5 Anakhazika mboni mwa Yakobo,
naika chilamulo mwa Israele,
ndizo analamulira atate athu,
akazidziwitse ana ao;
6 kuti mbadwo ukudzawo udziwe,
ndiwo ana amene akadzabadwa;
amene adzaimirira nadzafotokozera ana ao.
7 Ndi kuti chiyembekezo chao chikhale kwa Mulungu,
osaiwala zochita Mulungu,
koma kusunga malamulo ake ndiko.
8 Ndi kuti asange makolo ao,
ndiwo mbadwo woukirana ndi wopikisana ndi Mulungu;
mbadwo wosakonza mtima wao,
ndi mzimu wao sunakhazikike ndi Mulungu.
9 Ana a Efuremu okhala nazo zida, oponya nao mauta,
anabwerera m’mbuyo tsiku la nkhondo.
10 Sanasungachipanganocha Mulungu,
nakana kuyenda m’chilamulo chake.
11 Ndipo anaiwala zochita Iye,
ndi zodabwitsa zake zimene anawaonetsa.
12 Anachita chodabwitsa pamaso pa makolo ao,
m’dziko la Ejipito kuchidikha cha Zowani.
13 Anagawa nyanja nawapititsapo;
naimitsa madziwo ngati khoma.
14 Ndipo msana anawatsogolera ndi mtambo
ndi usiku wonse ndi kuunika kwa moto.
15 Anang’alula thanthwe m’chipululu,
ndipo anawamwetsa kochuluka monga m’madzi ozama.
16 Anatulukitsa mitsinje m’thanthwe,
inde anatsikitsa madzi ngati mitsinje.
17 Koma anaonjeza kumchimwira Iye,
kupikisana ndi Wam’mwambamwamba m’chipululu.
18 Ndipo anayesa Mulungu mumtima mwao
ndi kupempha chakudya monga mwa kulakalaka kwao.
19 Ndipo analankhula motsutsana ndi Mulungu;
anati, Kodi Mulungu akhoza kutikonzera podyera m’chipululu?
20 Taonani, anapanda thanthwe, ndi madzi anayendako
ndi mitsinje inasefuka;
kodi adzakhozanso kupatsa mkate?
Kodi adzafunira anthu ake nyama?
21 Chifukwa chake Yehova anamva, nakwiya;
ndipo anayatsa moto pa Yakobo,
ndiponso mkwiyo unakwera pa Israele.
22 Popeza sanakhulupirire Mulungu,
osatama chipulumutso chake.
23 Koma analamulira mitambo ili m’mwamba,
natsegula m’makomo a kumwamba.
24 Ndipo anawavumbitsiramana, adye,
nawapatsa tirigu wa kumwamba.
25 Yense anadya mkate wa angelo,
anawatumizira chakudya chofikira.
26 Anaombetsa m’mwamba mphepo ya kum’mawa,
natsogoza mwera ndi mphamvu yake.
27 Ndipo anawavumbitsira nyama ngati fumbi,
ndi mbalame zouluka ngati mchenga wa kunyanja.
28 Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,
pozungulira pokhala iwo.
29 Potero anadya nakhuta kwambiri;
ndipo anawapatsa chokhumba iwo.
30 Asanathe nacho chokhumba chao,
chakudya chao chili m’kamwa mwao,
31 pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,
ndipo anapha mwa onenepa ao,
nagwetsa osankhika a Israele.
32 Chingakhale ichi chonse anachimwanso,
osavomereza zodabwitsa zake.
33 Potero anathera masiku ao ndi zopanda pake,
ndi zaka zao mwa mantha.
34 Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;
nabwerera, nafunitsitsa Mulungu.
35 Ndipo anakumbukira kuti Mulungu ndiye thanthwe lao,
ndi Mulungu Wam’mwambamwamba Mombolo wao.
36 Koma anamsyasyalika pakamwa pao,
namnamiza ndi lilime lao.
37 Popeza mtima wao sunakonzekere Iye,
ndipo sanakhazikike m’chipangano chake.
38 Koma Iye pokhala ngwa chifundo,
anakhululukira choipa, osawaononga;
nabweza mkwiyo wake kawirikawiri,
sanautse ukali wake wonse.
39 Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu;
mphepo yopita yosabweranso.
40 Kawirikawiri nanga anapikisana ndi Iye kuchigwako,
nammvetsa chisoni m’chipululu.
41 Pakuti anabwerera m’mbuyo, nayesa Mulungu,
nachepsa Woyerayo wa Israele.
42 Sanakumbukire dzanja lake,
tsikuli anawaombola kwa msautsi.
43 Amene anaika zizindikiro zake mu Ejipito,
ndi zodabwitsa zake kuchidikha cha Zowani.
44 Nasanduliza nyanja yao mwazi,
ndi mitsinje yao, kuti sangakhoze kumwa.
45 Anawatumizira pakati pao mitambo ya ntchentche zakuwatha;
ndi achule akuwaononga.
46 Ndipo anapatsa mphuchi dzinthu dzao,
ndi dzombe ntchito yao.
47 Anapha mphesa zao ndi matalala,
ndi mikuyu yao ndi chisanu.
48 Naperekanso zoweta zao kwa matalala,
ndi ng’ombe zao kwa mphezi.
49 Anawatumizira mkwiyo wake wotentha,
kuzaza, ndi kupsa mtima, ndi nsautso,
ndizo gulu la amithenga ochita zoipa.
50 Analambulira mkwiyo wake njira;
sanalekerere moyo wao usafe,
koma anapereka moyo wao kumliri.
51 Ndipo anapha ana oyamba onse a mu Ejipito,
ndiwo oyamba a mphamvu yao m’mahema a Hamu.
52 Koma anatulutsa anthu ake ngati nkhosa,
nawatsogoza ngati gulu la zoweta m’chipululu.
53 Ndipo anawatsogolera mokhulupirika,
kotero kuti sanaope;
koma nyanja inamiza adani ao.
54 Ndipo anawafikitsa kumalire a malo ake oyera,
kuphiri ili, dzanja lamanja lake lidaligula.
55 Ndipo anapirikitsaamitundupamaso pao,
nawagawira cholowa chao, ndi muyeso,
nakhalitsa mafuko a Israele m’mahema mwao.
56 Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam’mwambamwamba,
osasunga mboni zake;
57 koma anabwerera m’mbuyo,
nachita zosakhulupirika monga makolo ao,
anapatuka ngati uta wolenda.
58 Ndipo anautsa mtima wake ndi malo amsanje ao,
namchititsa nsanje ndi mafano osema.
59 Pakumva ichi Mulungu, anakwiya,
nanyozatu Israele;
60 ndipo anachokera chokhalamo cha ku Silo,
chihemacho adachimanga mwa anthu;
61 napereka mphamvu yake mu ukapolo,
ndi ulemerero wake m’dzanja la msautsi.
62 Naperekanso anthu ake kwa lupanga;
nakwiya nacho cholowa chake.
63 Moto unapsereza anyamata ao;
ndi anamwali ao sanalemekezeke.
64 Ansembe ao anagwa ndi lupanga;
ndipo amasiye ao sanachite maliro.
65 Pamenepo Ambuye anauka ngati wam’tulo;
ngati chiphona chakuchita nthungululu ndi vinyo.
66 Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo;
nawapereka akhale otonzeka kosatha.
67 Tero anakana hema wa Yosefe;
ndipo sanasankhe fuko la Efuremu;
68 koma anasankha fuko la Yuda,
Phiri laZiyonilimene analikonda.
69 Ndipo anamanga malo oyera ake ngati kaphiri,
monga dziko lapansi limene analikhazikitsa kosatha.
70 Ndipo anasankha Davide mtumiki wake,
namtenga kumakola a nkhosa.
71 Anamtenga kuja anatsata zoyamwitsa,
awete Yakobo, anthu ake, ndi Israele, cholowa chake.
72 Potero anawaweta monga mwa mtima wake wangwiro;
nawatsogolera ndi luso la manja ake.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/78-e2156f04bd933a25a0454c3bfa7e9aca.mp3?version_id=1068—