Categories
MASALIMO

MASALIMO 50

Mulungu woweruza wa dziko lapansi

Salimo la Asafu.

1 Mulungu wa milungu, Yehova, wanena,

aitana dziko lapansi kuyambira kutuluka kwa dzuwa

kufikira kulowa kwake.

2 Mulungu awalira muZiyoni, mokongola mwangwiro.

3 Adzafika Mulungu wathu, ndipo sadzakhala chete.

Moto udzanyeka pankhope pake,

ndipo pozungulira pake padzasokosera kwakukulu.

4 Kumwamba adzaitana zakumwamba,

ndi dziko lapansi, kuti aweruze anthu ake.

5 Mundisonkhanitsire okondedwa anga,

amene anapangana ndi Ine ndi nsembe.

6 Ndipo zakumwamba zionetsera chilungamo chake;

pakuti Mulungu mwini wake ndiye woweruza.

7 Imvani, anthu anga, ndipo ndidzanena;

Israele, ndipo ndidzachita mboni pa iwe,

Ine Mulungu, ndine Mulungu wako.

8 Sindikudzudzula iwe chifukwa cha nsembe zako;

popeza nsembe zako zopsereza zili pamaso panga chikhalire.

9 Sindidzatenga ng’ombe m’nyumba mwako,

kapena mbuzi m’makola mwako.

10 Pakuti zamoyo zonse zakuthengo ndi zanga,

ndi ng’ombe za pa mapiri zikwi.

11 Ndidziwa mbalame zonse za m’mapiri,

ndipo nyama zakuthengo zili ndi Ine.

12 Ndikamva njala, sindidzakuuza,

pakuti dziko lonse ndi langa, ndi kudzala kwake komwe.

13 Kodi ndidzadya nyama ya ng’ombe,

kapena kumwa mwazi wa mbuzi?

14 Pereka kwa Mulungu nsembe yachiyamiko;

numchitire Wam’mwambamwamba chowinda chako.

15 Ndipo undiitane tsiku la chisautso,

ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.

16 Koma kwa woipa Mulungu anena,

Uli nao chiyani malemba anga kulalikira,

ndi kutchula pangano langa pakamwa pako?

17 Popeza udana nacho chilangizo,

nufulatira mau anga.

18 Pakuona mbala, uvomerezana nayo,

nuchita nao achigololo.

19 Pakamwa pako mpochita zochimwa,

ndipo lilime lako likonza chinyengo.

20 Ukhala, nuneneza mbale wako;

usinjirira mwana wa mai wako.

21 Izi unazichita iwe, ndipo ndinakhala chete Ine;

unayesa kuti ndifanana nawe,

ndidzakudzudzula, ndi kuchilongosola pamaso pako.

22 Dziwitsani ichi inu oiwala Mulungu,

kuti ndingakumwetuleni, ndipo mungasowepo mpulumutsi.

23 Wopereka nsembe yachiyamiko andilemekeza Ine;

ndipo kwa iye wosunga mayendedwe ake

ndidzamuonetsa chipulumutso cha Mulungu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/50-560e40fe908a0fdfb883d26be90e44ef.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 51

Davide avomereza kuchimwa kwake, apempha Mulungu amkhululukire, asamchotsere Mzimu Woyera

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide; m’mene anamdzera Natani mneneriyo atalowa iye kwa Bateseba.

1 Mundichitire ine chifundo, Mulungu,

monga mwa kukoma mtima kwanu;

monga mwa unyinji wa nsoni zanu zokoma

mufafanize machimo anga.

2 Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga,

ndipo mundiyeretse kundichotsera choipa changa.

3 Chifukwa ndazindikira machimo anga;

ndipo choipa changa chili pamaso panga chikhalire.

4 Pa Inu, Inu nokha, ndinachimwa,

ndipo ndinachichita choipacho pamaso panu;

kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu,

mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.

5 Onani, ndinabadwa m’mphulupulu,

ndipo mai wanga anandilandira m’zoipa.

6 Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m’malo a m’katimo;

ndipo m’malo a m’tseri mudzandidziwitsa nzeru.

7 Mundiyeretse ndihisopendipo ndidzayera;

munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbuu woposa matalala.

8 Mundimvetse chimwemwe ndi kusekera,

kuti mafupawo munawathyola akondwere.

9 Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga,

ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.

10 Mundilengere mtima woyera, Mulungu;

mukonze mzimu wokhazikika m’kati mwanga.

11 Musanditaye kundichotsa pamaso panu;

musandichotsere Mzimu wanu Woyera.

12 Mundibwezere chimwemwe cha chipulumutso chanu;

ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

13 Pomwepo ndidzalangiza ochimwa njira zanu;

ndipo olakwa adzabwera kwa Inu.

14 Mundilanditse kumlandu wa mwazi, Mulungu,

ndinu Mulungu wa chipulumutso changa;

lilime langa lidzakweza nyimbo ya chilungamo chanu.

15 Ambuye, tsegulani pa milomo yanga;

ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu.

16 Pakuti simukondwera ndi nsembe, mwenzi nditapereka;

nsembe yopsereza simuikonda.

17 Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka;

Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa.

18 ChitiraniZiyonichokoma monga mwa kukondwera kwanu;

mumange malinga a miyala aYerusalemu.

19 Pamenepo mudzakondwera nazo nsembe zachilungamo,

ndi nsembe yopsereza ndi yopsereza yathunthu;

pamenepo adzapereka

ng’ombe paguwa lanu la nsembe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/51-301c95ad4d072dd3013079c69eead3fa.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 52

Davide aneneratu za chionongeko cha oipa, iye nakhulupirira Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Chilangizo cha Davide; muja analowa Doegi Mwedomu nauza Saulo nati kwa iye, Davide walowa m’nyumba ya Ahimeleki.

1 Udzitamandiranji ndi choipa, chiphona iwe?

Chifundo cha Mulungu chikhala tsiku lonse.

2 Lilime lako likupanga zoipa;

likunga lumo lakuthwa, lakuchita monyenga.

3 Ukonda choipa koposa chokoma;

ndi bodza koposa kunena chilungamo,

4 ukonda mau onse akuononga,

lilime lachinyengo, iwe.

5 Potero Mulungu adzakupasula kunthawi zonse,

adzakuchotsa nadzakukwatula m’hema mwako,

nadzakuzula, kukuchotsa m’dziko la amoyo.

6 Ndipo olungama adzachiona, nadzaopa,

nadzamseka, ndi kuti,

7 Tapenyani, suyu munthuyu amene sanamuyese Mulungu mphamvu yake;

amene anatama kuchuluka kwa chuma chake,

nadzilimbitsa m’kuipsa kwake.

8 Koma ine ndine ngati mtengo wauwisi waazitona

m’nyumba ya Mulungu.

Ndikhulupirira chifundo cha Mulungu kunthawi za nthawi.

9 Ndidzakuyamikani kosatha, popeza Inu munachichita ichi,

ndipo ndidzayembekeza dzina lanu, pakuti ichi nchokoma,

pamaso pa okondedwa anu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/52-714c69d5d39300a0a025329eac12d0ed.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 53

Kupusa ndi kuipa kwa anthu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Mahalati. Chilangizo cha Davide.

1 Chitsiru chimati mumtima mwake, Kulibe Mulungu.

Achita zovunda, achita chosalungama chonyansa;

kulibe wakuchita bwino.

2 Mulungu m’mwamba anaweramira pa ana a anthu,

kuti aone ngati aliko wanzeru,

wakufuna Mulungu.

3 Onse anabwerera; anavunda mtima pamodzi;

palibe mmodzi wakuchita bwino, nnena mmodzi.

4 Kodi ochita zopanda pake sadziwa?

Pomadya anthu anga monga akudya mkate;

ndipo saitana Mulungu.

5 Pamenepo anaopa kwakukulu, popanda chifukwa cha kuopa,

pakuti Mulungu anamwaza mafupa a iwo akuzinga iwe;

unawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawakaniza.

6 Ha, chipulumutso cha Israele chichokere muZiyoni!

Pakubweretsa Mulungu anthu ake a m’ndende,

Yakobo adzakondwera, Israele adzasekera.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/53-f695e745f1b28f07ca0f2bd5d9677d56.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 54

Davide apempha Mulungu amlanditse

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Chilangizo cha Davide. Muja Azifi anamuka nauza Saulo, kuti, Kodi Davide sabisala kwathu nanga?

1 Ndipulumutseni, Mulungu, mwa dzina lanu,

ndipo mundiweruze ndi mphamvu yanu.

2 Imvani pemphero langa, Mulungu;

tcherani khutu mau a pakamwa panga.

3 Pakuti alendo andiukira,

ndipo oopsa afunafuna moyo wanga;

sadziikira Mulungu pamaso pao.

4 Taonani, Mulungu ndiye mthandizi wanga,

Ambuye ndiye wachirikiza moyo wanga.

5 Adzabwezera choipa adani anga,

aduleni m’choonadi chanu.

6 Ine mwini ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu,

ndidzayamika dzina lanu, Yehova, pakuti nlokoma.

7 Pakuti anandilanditsa m’nsautso yonse;

ndipo ndapenya ndi diso langa icho ndakhumbira pa adani anga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/54-7e0db2663d17ad9db483aea5e9664885.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 55

Davide adandaula pa kuipa kwa adani, adziponya kwa Mulungu, nalangiza ena azitero iwo omwe

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Chilangizo cha Davide.

1 Tcherani khutu pemphero langa, Mulungu;

ndipo musadzibisa pa kupemba kwanga.

2 Mverani, ndipo mundiyankhe,

ndiliralira m’kudandaula kwanga ndi kubuula;

3 chifukwa cha mau a mdani,

chifukwa cha kundipsinja woipa;

pakuti andisenza zopanda pake,

ndipo adana nane mumkwiyo.

4 Mtima wanga uwawa m’kati mwanga;

ndipo zoopsa za imfa zandigwera.

5 Mantha ndi kunjenjemera zandidzera,

ndipo zoopsetsa zandikuta.

6 Ndipo ndinati, Ha, wina akadandipatsa mapiko onga a njiwa!

Mwenzi nditauluka, ndi kukhaliratu.

7 Onani, ndikadathawira kutali,

ndikadagona m’chipululu.

8 Ndikadafulumira ndipulumuke

kumphepo yolimba ndi namondwe.

9 Aonongeni, Ambuye, gawani lilime lao,

pakuti ndaona chiwawa ndi ndeu m’mzindamo.

10 Izizo ziuzungulira pa malinga ake usana ndi usiku;

ndipo m’kati mwake muli zopanda pake ndi chovuta.

11 M’kati mwake muli kusakaza,

chiwawa ndi chinyengo sizichoka m’makwalala ake.

12 Pakuti si mdani amene ananditonzayo;

pakadatero ndikadachilola,

amene anadzikuza pa ine sindiye munthu wondida;

pakadatero ndikadambisalira:

13 Koma ameneyo ndiwe, munthu woyenerana nane,

tsamwali wanga, wodziwana nane.

14 Tinapangirana upo wokoma,

tinaperekeza khamu la anthu popita kunyumba ya Mulungu.

15 Imfa iwagwere modzidzimutsa,

atsikire kumanda ali amoyo,

pakuti m’mokhala mwao muli zoipa pakati pao.

16 Koma ine ndidzafuulira kwa Mulungu;

ndipo Yehova adzandipulumutsa.

17 Madzulo, m’mawa, ndi msana ndidzadandaula, ndi kubuula,

ndipo adzamva mau anga.

18 Anaombola moyo wanga kunkhondo,

ndikhale mumtendere,

pakuti ndiwo ambiri okangana nane.

19 Mulungu adzamva, nadzawasautsa,

ndiye wokhalabe chiyambire kale lomwe.

Popeza iwowa sasinthika konse,

ndipo saopa Mulungu.

20 Anatulutsa manja ake awagwire iwo akuyanjana naye,

anaipsa pangano lake.

21 Pakamwa pake mposalala ngati mafuta amkaka,

koma mumtima mwake munali nkhondo,

mau ake ngofewa ngati mafuta oyenga,

koma anali malupanga osololasolola.

22 Umsenze Yehova nkhawa zako, ndipo Iye adzakugwiriziza,

nthawi zonse sadzalola wolungama agwedezeke.

23 Koma Inu, Mulungu, mudzawatsitsira kudzenje la chionongeko.

Anthu okhetsa mwazi ndi achinyengo masiku ao sadzafikira nusu;

koma ine ndidzakhulupirira Inu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/55-f6f43717a2860f3b667923d0cea61273.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 56

Davide apempha Mulungu amlanditse; ayamika atamlanditsa

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Yonat-Elem-Rekokimu. Mikitamu wa Davide; muja Afilisti anamgwira mu Gati.

1 Mundichitire chifundo, Mulungu, pakuti anthu afuna kundimeza.

Andipsinja pondithira nkhondo tsiku lonse.

2 Adani anga afuna kundimeza tsiku lonse,

pakuti ambiri andithira nkhondo modzikuza.

3 Tsiku lakuopa ine,

ndidzakhulupirira Inu.

4 Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ake,

ndakhulupirira Mulungu, sindidzaopa;

anthu adzandichitanji?

5 Tsiku lonse atenderuza mau anga,

zolingirira zao zonse zili pa ine kundichitira choipa.

6 Amemezana, alalira,

atchereza mapazi anga,

popeza alindira moyo wanga.

7 Kodi adzapulumuka ndi zopanda pake?

Gwetsani anthu mumkwiyo, Mulungu.

8 Muwerenga kuthawathawa kwanga,

sungani misozi yanga m’nsupa yanu;

kodi siikhala m’buku mwanu?

9 Pamenepo adani anga adzabwerera m’mbuyo tsiku lakuitana ine.

Ichi ndidziwa, kuti Mulungu avomerezana nane.

10 Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ake,

mwa Yehova ndidzalemekeza mau ake.

11 Pa Mulungu ndakhulupirira, sindidzaopa;

munthu adzandichitanji?

12 Zowindira Inu Mulungu, zili pa ine,

ndidzakuchitirani zoyamika.

13 Pakuti mwalanditsa moyo wanga kuimfa,

simunatero nao mapazi anga kuti ndingagwe?

Kuti ndiyende pamaso pa Mulungu

m’kuunika kwa amoyo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/56-87c25ca541a0a6dc7b071d0a07c0ab37.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 57

Davide apempha Mulungu amtchinjirize, namlemekezapo

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Altasheti. Mikitamu wa Davide; muja anathawa Saulo, ali m’phanga.

1 Mundichitire chifundo, Mulungu, mundichitire chifundo;

pakuti moyo wanga ukhulupirira Inu,

ndipo ndithawira kumthunzi wa mapiko anu,

kufikira zosakazazo zidzapita.

2 Ndidzafuulira kwa Mulungu Wam’mwambamwamba;

ndiye Mulungu wonditsirizira zonse.

3 Adzanditumizira m’mwamba, nadzandipulumutsa

ponditonza wofuna kundimeza;

Mulungu adzatumiza chifundo chake ndi choonadi chake.

4 Moyo wanga uli pakati pa mikango;

ndigona pakati pa oyaka moto,

ndiwo ana a anthu amene mano ao ali nthungo ndi mivi,

ndipo lilime lao ndilo lupanga lakuthwa.

5 Mukwezeke m’mwambamwamba, Mulungu;

ulemerero wanu ukhale pamwamba padziko lonse lapansi.

6 Ananditchera ukonde apo ndiyenda;

moyo wanga wawerama.

Anandikumbira mbuna patsogolo panga;

anagwa m’kati mwake iwo okha.

7 Mtima wanga wakhazikika, Mulungu, ndakhazika mtima;

ndidzaimba, inde, ndidzaimba zolemekeza.

8 Galamuka, ulemu wanga; galamukani chisakasa ndi zeze!

Ndidzauka ndekha mamawa.

9 Ndidzakuyamikirani mwa anthu, Ambuye,

ndidzakuimbirani mwa mitundu.

10 Pakuti chifundo chanu nchachikulu kufikira m’mwamba,

ndi choonadi chanu kufikira mitambo.

11 Kwezekani m’mwambamwamba, Mulungu;

ulemerero wanu ukhale pamwamba m’dziko lonse lapansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/57-b8e32b44aecaea2420ecc0fbf388b73f.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 58

Davide adzudzula oipa Mulungu awalange

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Altasyeti. Mikitamu wa Davide.

1 Kodi muli chete ndithu poyenera inu kunena zolungama?

Muweruza ana anthu molunjika kodi?

2 Inde, mumtima muchita zosalungama;

padziko lapansi mugawira anthu chiwawa cha m’manja mwanu.

3 Oipa achita chilendo chibadwire,

asokera kuyambira kubadwa kwao, nanena bodza.

4 Ululu wao ukunga wa njoka;

akunga mphiri yogontha m’khutu, itseka m’khutu mwake.

5 Imene siimvera liu la oitana,

akuchita matsenga mochenjeratu.

6 Thyolani mano ao m’kamwa mwao, Mulungu,

zulani zitsakano za misona ya mkango, Yehova.

7 Apitetu ngati madzi oyenda;

popiringidza mivi yake ikhale yodukaduka.

8 Apite ngati nkhono yosungunuka;

asaone dzuwa monga mtayo.

9 Miphika yanu isanagwire moto waminga,

adzaiuluza, yaiwisi ndi yoyaka.

10 Wolungama adzakondwera pakuona kubwezera chilango,

adzasamba mapazi ake m’mwazi wa woipa.

11 Ndipo anthu adzati, Indedi, pali mphotho kwa wolungama.

Indedi, pali Mulungu wakuweruza padziko lapansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/58-b824fc7f69079b8cbb5de62ba641a2a6.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 59

Davide apempha Mulungu amlanditse, nadzinenera wosalakwa

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Altasheti. Mikitamu wa Davide; muja Saulo anatuma anthu adikire nyumba yake, kuti amuphe.

1 Ndilanditseni kwa adani anga, Mulungu wanga,

ndiikeni pamsanje kwa iwo akundiukira.

2 Mundilanditse kwa ochita zopanda pake,

ndipo ndipulumutseni kwa anthu olira mwazi.

3 Pakuti onani, alalira moyo wanga;

amphamvu andipangira chiwembu,

osachimwa, osalakwa ine, Yehova,

4 osawapatsa chifukwa ine, athamanga nadzikonza.

Galamukani kukomana nane, ndipo penyani.

5 Ndinu Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israele.

Ukani kukazondaamitunduonse,

musachitire chifundo mmodzi yense

wakuchita zopanda pake monyenga.

6 Abwera madzulo, auwa ngati galu,

nazungulira mzinda.

7 Onani abwetuka pakamwa pao;

m’milomo mwao muli lupanga,

pakuti amati, Amva ndani?

8 Koma Inu, Yehova, mudzawaseka;

mudzalalatira amitundu onse.

9 Inu, mphamvu yanga, ndidzakulindirani;

pakuti Mulungu ndiye msanje wanga.

10 Mulungu wa chifundo changa adzandichingamira,

adzandionetsa tsoka la adani anga.

11 Musawapheretu, angaiwale anthu anga,

muwabalalitse mwa mphamvu yanu, ndipo muwagwetse,

Ambuye, ndinu chikopa chathu.

12 Pakamwa pao achimwa ndi mau onse a pa milomo yao,

potero akodwe m’kudzitamandira kwao,

ndiponso chifukwa cha kutemberera ndi bodza azilankhula.

13 Muwathe mumkwiyo, muwagulule psiti.

Ndipo adziwe kuti Mulungu ndiye woweruza mu Yakobo,

kufikira malekezero a dziko la pansi.

14 Ndipo abwere madzulo, auwe ngati galu,

nazungulire mzinda.

15 Ayendeyende ndi kufuna chakudya,

nachezere osakhuta.

16 Koma ine, ndidzaimbira mphamvu yanu;

inde ndidzaimbitsa chifundo chanu mamawa,

pakuti Inu mwakhala msanje wanga,

ndi pothawirapo ine tsiku la nsautso yanga.

17 Ndidzaimbira zakukulemekezani Inu, mphamvu yanga;

pakuti Mulungu ndiye msanje wanga,

Mulungu wa chifundo changa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/59-e89d78b60b007ab882f1c5c2366da500.mp3?version_id=1068—