Categories
MASALIMO

MASALIMO 30

Mkwiyo wa Mulungu ukhala kanthawi, kuyanja kwao ndi kosatha

Salimo la Davide. Nyimbo yakuperekera nyumba kwa Mulungu.

1 Ndidzakukwezani, Yehova; pakuti mwandinyamutsa,

ndipo simunandikondwetsere adani anga.

2 Yehova, Mulungu wanga,

ndinafuulira kwa Inu, ndipo munandichiritsa.

3 Yehova munabweza moyo wanga kumanda,

munandisunga ndi moyo, kuti ndingatsikire kudzenje.

4 Imbirani Yehova, inu okondedwa ake,

ndipo yamikani pokumbukira chiyero chake.

5 Pakuti mkwiyo wake ukhala kanthawi kokha;

koma kuyanja kwake moyo wonse.

Kulira kuchezera,

koma mamawa kuli kufuula kokondwera.

6 Ndipo ine, ndinanena m’phindu langa,

sindidzagwedezeka nthawi zonse.

7 Inu, Yehova, munakhazikitsa phiri langa ndi kuyanja kwanu;

munabisa nkhope yanu; ndinaopa.

8 Ndinafuulira kwa Inu, Yehova;

kwa Ambuye ndinapemba,

9 M’mwazi mwanga muli phindu lanji,

potsikira ine kudzenje?

Ngati fumbi lidzayamika Inu?

Ngati lidzalalikira choonadi chanu?

10 Mverani, Yehova, ndipo ndichitireni chifundo,

Yehova, mundithandize ndi Inu.

11 Munasanduliza kulira kwanga kukhale kusekera;

munandivula chiguduli changa, ndipo munandiveka chikondwero,

12 kuti ulemu wanga uimbire Inu, wosakhala chete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/30-94c410991fb6fa5a91232c2b3b49d4ac.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 31

Davide apempha kolimba Mulungu amlanditse, natama chifundo chao, nauzitsa anthu a Mulungu amtame

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Ndakhulupirira Inu, Yehova,

ndikhale wopanda manyazi nthawi zonse,

mwa chilungamo chanu ndipulumutseni ine.

2 Munditcherere khutu lanu; ndipulumutseni msanga.

Mundikhalire ine thanthwe lolimba,

nyumba yamalinga yakundisunga.

3 Pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa;

ndipo chifukwa cha dzina lanu

ndiyendetseni bwino, ndipo nditsogolereni.

4 Mundionjole mu ukonde umene ananditchera mobisika.

Pakuti Inu ndinu mphamvu yanga.

5 Ndipereka mzimu wanga m’dzanja lanu;

mwandiombola, Inu Yehova, Mulungu wa choonadi.

6 Ndikwiya nao iwo akusamala zachabe zonama,

koma ndikhulupirira Yehova.

7 Ndidzakondwera ndi kusangalala m’chifundo chanu,

pakuti mudapenya zunzo langa;

ndipo mudadziwa mzimu wanga mu nsautso yanga.

8 Ndipo simunandipereke m’dzanja la mdani;

munapondetsa mapazi anga pali malo.

9 Mundichitire chifundo, Yehova, pakuti ndasautsika ine.

Diso langa, mzimu wanga, ndi mimba yanga,

zapuwala ndi mavuto.

10 Pakuti moyo wanga watha ndi chisoni,

ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo.

Mphamvu yanga yafooka chifukwa cha kusakaza kwanga,

ndi mafupa anga apuwala.

11 Ndakhala chotonza chifukwa cha akundisautsa onse,

inde, koposa kwa anansi anga; ndipo anzanga andiyesa choopsa;

iwo akundipenya pabwalo anandithawa.

12 Ndaiwalika m’mtima monga wakufa,

ndikhala monga chotengera chosweka.

13 Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri,

mantha andizinga.

Pondipangira chiwembu,

anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.

14 Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova,

ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga.

15 Nyengo zanga zili m’manja mwanu,

mundilanditse m’manja a adani anga,

ndi kwa iwo akundilondola ine.

16 Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu,

mundipulumutse ndi chifundo chanu.

17 Yehova, musandichititse manyazi; pakuti ndafuulira kwa Inu,

oipa achite manyazi, atonthole m’manda.

18 Ikhale yosalankhula milomo ya mabodza,

imene imalankhula mwachipongwe pa olungama mtima,

ndi kudzikuza ndi kunyoza.

19 Ha! Kukoma kwanu ndiko kwakukulu nanga,

kumene munasungira iwo akuopa Inu,

kumene munachitira iwo akukhulupirira Inu,

pamaso pa ana a anthu!

20 Pobisalira pamaso panu mudzawabisa kwa chiwembu cha munthu,

mudzawabisa iwo mumsasa kuti muwalanditse

pa kutetana kwa malilime.

21 Wolemekezeka Yehova,

pakuti anandichitira chifundo chake chodabwitsa

m’mzinda walinga.

22 Ndipo ine, pakutenga nkhawa, ndinati,

Ndadulidwa kundichotsa pamaso panu.

Komatu munamva mau a kupemba kwanga

pamene ndinafuulira kwa Inu.

23 Kondani Yehova, Inu nonse okondedwa ake,

Yehova asunga okhulupirika,

ndipo abwezera zochuluka iye wakuchita zodzitama.

24 Limbikani ndipo Iye adzalimbitsa mtima wanu,

inu nonse akuyembekeza Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/31-95e6f9d75c35ecc2076f587382352d82.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 32

Mwai wa munthu amene Mulungu wamkhululukira

Salimo la Davide. Chilangizo.

1 Wodala munthuyo wokhululukidwa tchimo lake;

wokwiriridwa choipa chake.

2 Wodala munthuyu Yehova samwerengera mphulupulu zake;

ndimo mumzimu mwake mulibe chinyengo.

3 Pamene ndinakhala chete mafupa anga anakalamba

ndi kubuula kwanga tsiku lonse.

4 Chifukwa usana ndi usiku dzanja lanu linandilemera ine;

uwisi wanga unasandulika kuuma kwa malimwe.

5 Ndinavomera choipa changa kwa Inu;

ndipo mphulupulu yanga sindinaibise.

Ndinati, Ndidzaululira Yehova machimo anga;

ndipo munakhululukira choipa cha kulakwa kwanga.

6 Chifukwa chake oyera mtima onse apemphere kwa Inu,

pa nthawi ya kupeza Inu;

indetu pakusefuka madzi aakulu

sadzamfikira iye.

7 Inu ndinu mobisalira mwanga;

m’nsautso mudzandisunga;

mudzandizinga ndi nyimbo za chipulumutso.

8 Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo;

ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang’ana iwe.

9 Musakhale monga kavalo, kapena ngati bulu, wopanda nzeru;

zomangira zao ndizo cham’kamwa ndi chapamutu zakuwakokera,

pakuti ukapanda kutero sadzakuyandikiza.

10 Zisoni zambiri zigwera woipa;

koma chifundo chidzamzinga iye wakukhulupirira Yehova.

11 Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima;

ndipo fuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/32-8b62cf41b1629155077301dc08c38e74.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 33

Alemekeza Mulungu wolenga, wosunga zonse

1 Fuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima,

oongoka mtima ayenera kulemekeza.

2 Yamikani Yehova ndi zeze;

muimbireni ndi chisakasa cha zingwe khumi.

3 Mumuimbire Iye nyimbo yatsopano;

muimbe mwaluso kumveketsa mau.

4 Pakuti mau a Yehova ali olunjika;

ndi ntchito zake zonse zikhulupirika.

5 Iye ndiye wakukonda chilungamo ndi chiweruzo,

dziko lapansi ladzala ndi chifundo cha Yehova.

6 Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova;

ndipo ndi mpweya wa m’kamwa mwake khamu lao lonse.

7 Amaunjika madzi a m’nyanja monga mulu,

amakundika zakudya mosungiramo.

8 Dziko lonse lapansi liope Yehova,

ponse pali anthu achite mantha chifukwa cha Iye.

9 Pakuti ananena, ndipo chinachitidwa;

analamulira, ndipo chinakhazikika.

10 Yehova aphwanya upo waamitundu,

asandutsa chabe zolingirira za mitundu ya anthu.

11 Chiweruzo cha Yehova chikhazikika chikhazikikire,

zolingirira za m’mtima mwake ku mibadwomibadwo.

12 Wodalitsika mtundu wa anthu

umene Yehova ndiye Mulungu wao;

mtundu womwe anausankha ukhale cholowa cha Iye yekha.

13 Yehova apenyerera m’mwamba;

aona ana onse a anthu.

14 M’malo akhalamo Iye, amapenya pansi

pa onse akukhala m’dziko lapansi.

15 Iye amene akonza mitima ya iwo onse,

amene azindikira zochita zao zonse.

16 Palibe mfumu yoti gulu lalikulu limpulumutsa,

mphamvu yaikulu siichilanditsa chiphona.

17 Kavalo safikana kupulumuka naye,

chinkana mphamvu yake njaikulu sapulumutsa.

18 Taonani, diso la Yehova lili pa iwo akumuopa Iye,

pa iwo akuyembekeza chifundo chake.

19 Kupulumutsa moyo wao kwa imfa,

ndi kuwasunga ndi moyo m’nyengo ya njala.

20 Moyo wathu walindira Yehova;

Iye ndiye thandizo lathu ndi chikopa chathu.

21 Pakuti mtima wathu udzakondwera mwa Iye,

chifukwa takhulupirira dzina lake loyera.

22 Yehova, chifundo chanu chikhale pa ife,

monga takuyembekezani Inu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/33-290a5e48f820310e3fb6c329165e9f93.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 34

Davide alemekeza Yehova womlanditsa, nafulumiza ena amtame

Salimo la Davide; muja anasintha makhalidwe ake pamaso pa Abimeleki, amene anampirikitsa, ndipo anachoka.

1 Ndidzalemekeza Yehova nyengo zonse;

kumlemekeza kwake kudzakhala m’kamwa mwanga kosalekeza.

2 Moyo wanga udzatamanda Yehova;

ofatsa adzakumva nadzakondwera.

3 Bukitsani pamodzi ndine ukulu wa Yehova,

ndipo tikweze dzina lake pamodzi.

4 Ndinafuna Yehova ndipo anandivomera,

nandilanditsa m’mantha anga onse.

5 Iwo anayang’ana Iye nasanguluka;

ndipo pankhope pao sipadzachita manyazi.

6 Munthu uyu wozunzika anafuula, ndipo Yehova anamumva,

nampulumutsa m’masautso ake onse.

7 Mngelowa Yehova azinga kuwatchinjiriza iwo akuopa Iye,

nawalanditsa iwo.

8 Talawani, ndipo onani kuti Yehova ndiye wabwino;

wodala munthuyo wakukhulupirira Iye.

9 Opani Yehova, inu oyera mtima ake;

chifukwa iwo akumuopa Iye sasowa.

10 Misona ya mkango isowa nimva njala,

koma iwo akufuna Yehova sadzasowa kanthu kabwino.

11 Idzani ananu ndimvereni ine,

ndidzakulangizani zakumuopa Yehova.

12 Munthu wokhumba moyo ndani,

wokonda masiku, kuti aone zabwino?

13 Uletse lilime lako lisatchule zoipa,

ndipo milomo yako isalankhule chinyengo.

14 Futuka pazoipa, nuchite zabwino,

funa mtendere ndi kuulondola.

15 Maso a Yehova ali pa olungama mtima,

ndipo makutu ake atchereza kulira kwao.

16 Nkhope ya Yehova itsutsana nao akuchita zoipa,

kudula chikumbukiro chao padziko lapansi.

17 Iwowo anaitana, ndipo Yehova anawamva,

nawalanditsa kumasautso ao onse.

18 Yehova ali pafupi ndi iwo a mtima wosweka,

apulumutsa iwo a mzimu wolapadi.

19 Masautso a wolungama mtima achuluka,

koma Yehova amlanditsa mwa onsewa.

20 Iye asunga mafupa ake onse;

silinathyoke limodzi lonse.

21 Mphulupulu idzamupha woipa;

ndipo adzawatsutsa kumlandu iwo akudana naye wolungama.

22 Yehova aombola moyo wa anyamata ake,

ndipo sadzawatsutsa kumlandu onse akukhulupirira Iye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/34-fddb50ecc3982b4253380c39b2d29221.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 35

Davide apempha Mulungu alange oipa

Salimo la Davide.

1 Tsutsanani nao iwo akutsutsana nane, Yehova;

limbanani nao iwo akulimbana nane.

2 Gwirani chikopa chotchinjiriza,

ukani kundithandiza.

3 Sololani nthungo, ndipo muwatsekerezere kunjira akundilondola.

Nenani ndi moyo wanga,

Chipulumutso chako ndine.

4 Athe nzeru nachite manyazi iwo akufuna moyo wanga;

abwezedwe m’mbuyo nasokonezeke iwo akundipangira chiwembu.

5 Akhale monga mungu kumphepo,

ndipomngelowa Yehova awapirikitse.

6 Njira yao ikhale ya mdima ndi yoterera,

ndipo mngelo wa Yehova awalondole.

7 Pakuti ananditchera ukonde wao m’mbunamo kopanda chifukwa,

anakumbira moyo wanga dzenje kopanda chifukwa.

8 Chimgwere modzidzimutsa chionongeko;

ndipo ukonde wake umene anautcha umkole yekha mwini,

agwemo, naonongeke m’mwemo.

9 Ndipo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova;

udzasekera mwa chipulumutso chake.

10 Mafupa anga onse adzanena,

Yehova, afanana ndi Inu ndani,

wakulanditsa wozunzika kwa iye amene amposa mphamvu,

ndi wozunzika ndi waumphawi kwa iye amfunkhira?

11 Mboni za chiwawa ziuka,

zindifunsa zosadziwa ine.

12 Andibwezera choipa m’malo mwa chokoma,

inde, asaukitsa moyo wanga.

13 Koma ine, pakudwala iwowa, chovala changa ndi chiguduli.

Ndinazunza moyo wanga ndi kusala;

ndipo pemphero langa linabwera kuchifuwa changa.

14 Ndakhala ine monga ngati iye anali bwenzi langa,

kapena mbale wanga;

polira ndinaweramira pansi,

monga munthu wakulira maliro amai wake.

15 Ndipo pakutsimphina ine anakondwera,

nasonkhana pamodzi;

akundipanda anandisonkhanira; ndipo sindinachidziwe,

ananding’amba osaleka.

16 Pakati pa onyodola pamadyerero,

anandikukutira mano.

17 Ambuye, mudzapenyererabe nthawi yanji?

Bwezani moyo wanga kwa zakundiononga zao,

wanga wa wokha kwa misona ya mkango.

18 Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;

m’chikhamu cha anthu ndidzakulemekezani.

19 Adani anga asandikondwerere ine monyenga;

okwiya nane kopanda chifukwa asanditsinzinire.

20 Pakuti salankhula zamtendere,

koma apangira chiwembu odekha m’dziko.

21 Ndipo andiyasamira m’kamwa mwao;

nati, Hede, Hede, diso lathu lidachipenya.

22 Yehova, mudazipenya; musakhale chete,

Ambuye, musakhale kutali ndi ine.

23 Galamukani, ndipo khalani maso kundiweruzira mlandu wanga,

Mulungu wanga ndi Ambuye wanga.

24 Mundiweruze monga mwa chilungamo chanu,

Yehova Mulungu wanga;

ndipo asandisekerere ine.

25 Asanene mumtima mwao, Hede, momwemo!

Asanene, Tammeza iye.

26 Achite manyazi, nadodome iwo akukondwera

chifukwa cha choipa chidandigwera.

Avekeke ndi manyazi ndi kupunzika iwo akudzikuza pa ine.

27 Afuule mokondwera nasangalale

iwo akukondwera nacho chilungamo changa,

ndipo anene kosalekeza, Abuke Yehova,

amene akondwera ndi mtendere wa mtumiki wake.

28 Ndipo lilime langa lilalikire chilungamo chanu,

ndi lemekezo lanu tsiku lonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/35-5ad349840a1959a8937cc9073d44af98.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 36

Kuipitsitsa kwa anthu, kukometsetsa kwa Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova.

1 Cholakwa cha woipayo chimati m’kati mwa mtima wanga,

palibe kuopa Mulungu pamaso pake.

2 Pakuti adzidyoletsa yekha m’kuona kwake,

kuti anthu sadzachipeza choipa chake ndi kukwiya nacho.

3 Mau a pakamwa pake ndiwo opanda pake ndi onyenga,

waleka kuzindikira ndi kuchita bwino.

4 Alingirira zopanda pake pakama pake;

adziika panjira posati pabwino;

choipa saipidwa nacho.

5 Yehova, m’mwamba muli chifundo chanu;

choonadi chanu chifikira kuthambo.

6 Chilungamo chanu chikunga mapiri a Mulungu;

maweruzo anu akunga chozama chachikulu,

Yehova, musunga munthu ndi nyama.

7 Ha! Chifundo chanu, Mulungu, nchokondedwadi!

Ndipo ana a anthu athawira kumthunzi wa mapiko anu.

8 Adzakhuta kwambiri ndi zonona za m’nyumba mwanu,

ndipo mudzawamwetsa mu mtsinje wa zokondweretsa zanu.

9 Pakuti chitsime cha moyo chili ndi Inu,

M’kuunika kwanu tidzaona kuunika.

10 Tanimphitsani chifundo chanu pa iwo akudziwa Inu;

ndi chilungamo chanu pa oongoka mtima.

11 Phazi la akudzikuza lisandifikire ine,

ndi dzanja la oipa lisandichotse.

12 Pomwepo padagwera ochita zopanda pake.

Anawalikha, ndipo sadzatha kuukanso.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/36-41066793019d717dbea4c3065b406512.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 37

Kusangalala kwa ochimwa kudzatha, olungama akhalitsa nathandizidwa ndi Mulungu

Salimo la Davide.

1 Usavutike mtima chifukwa cha ochita zoipa,

usachite nsanje chifukwa cha ochita chosalungama.

2 Pakuti adzawamweta msanga monga udzu,

ndipo adzafota monga msipu wauwisi.

3 Khulupirira Yehova, ndipo chita chokoma;

khala m’dziko, ndipo tsata choonadi.

4 Udzikondweretsenso mwa Yehova;

ndipo Iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

5 Pereka njira yako kwa Yehova;

khulupiriranso Iye, adzachichita.

6 Ndipo adzaonetsa chilungamo chako monga kuunika,

ndi kuweruza kwako monga usana.

7 Khala chete mwa Yehova, numlindirire Iye;

usavutike mtima chifukwa cha iye wolemerera m’njira yake,

chifukwa cha munthu wakuchita chiwembu.

8 Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo;

usavutike mtima ungachite choipa.

9 Pakuti ochita zoipa adzadulidwa;

koma iwo akuyembekeza Yehova,

iwowa adzalandira dziko lapansi.

10 Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti;

inde, udzayang’anira mbuto yake, nudzapeza palibe.

11 Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi;

nadzakondwera nao mtendere wochuluka.

12 Woipa apangira chiwembu wolungama,

namkukutira mano.

13 Ambuye adzamseka,

popeza apenya kuti tsiku lake likudza.

14 Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao;

alikhe ozunzika ndi aumphawi,

aphe amene ali oongoka m’njira.

15 Lupanga lao lidzalowa m’mtima mwao momwe,

ndipo mauta ao adzathyoledwa.

16 Zochepa zake za wolungama zikoma

koposa kuchuluka kwao kwa oipa ambiri.

17 Pakuti manja a oipa adzathyoledwa,

koma Yehova achirikiza olungama.

18 Yehova adziwa masiku a anthu angwiro;

ndipo cholowa chao chidzakhala chosatha.

19 Sadzachita manyazi m’nyengo yoipa,

ndipo m’masiku a njala adzakhuta.

20 Pakuti oipa adzatayika,

ndipo adani ake a Yehova adzanga mafuta a anaankhosa;

adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.

21 Woipa akongola, wosabweza,

koma wolungama achitira chifundo, napereka.

22 Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;

koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.

23 Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;

ndipo akondwera nayo njira yake.

24 Angakhale akagwa, satayikiratu,

pakuti Yehova agwira dzanja lake.

25 Ndinali mwana ndipo ndakalamba;

ndipo sindinapenye wolungama atasiyidwa,

kapena mbumba zake zilinkupempha chakudya.

26 Tsiku lonse achitira chifundo, nakongoletsa;

ndipo mbumba zake zidalitsidwa.

27 Siyana nacho choipa, nuchite chokoma,

nukhale nthawi zonse.

28 Pakuti Yehova akonda chiweruzo,

ndipo sataya okondedwa ake.

Asungika kosatha,

koma adzadula mbumba za oipa.

29 Olungama adzalandira dziko lapansi,

nadzakhala momwemo kosatha.

30 Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru,

ndi lilime lake linena chiweruzo.

31 Malamulo a Mulungu wake ali mumtima mwake;

pakuyenda pake sadzaterereka.

32 Woipa aunguza wolungama,

nafuna kumupha.

33 Yehova sadzamsiya m’dzanja lake;

ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.

34 Yembekeza Yehova, nusunge njira yake,

ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko.

Pakudulidwa oipa udzapenya.

35 Ndapenya woipa, alikuopsa,

natasa monga mtengo wauwisi wanzika.

36 Koma anapita ndipo taona, kwati zii;

ndipo ndinampwaira osampeza.

37 Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima!

Pakuti ku matsiriziro ake a munthuyo kuli mtendere.

38 Koma olakwa adzaonongeka pamodzi;

matsiriziro a oipa adzadulidwa.

39 Koma chipulumutso cha olungama chidzera kwa Yehova,

Iye ndiye mphamvu yao m’nyengo ya nsautso.

40 Ndipo Yehova awathandiza, nawalanditsa;

awalanditsa kwa oipa nawapulumutsa,

chifukwa kuti anamkhulupirira Iye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/37-b05a1f859375b97fcce3087bbc69abe3.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 38

Davide awulula zoipa zake, apempha Mulungu amkhululukire namthandize

Salimo la Davide, lakukumbutsa.

1 Yehova, musandidzudzule ndi mkwiyo wanu,

ndipo musandilange moopsa m’mtima mwanu.

2 Pakuti mivi yanu yandilowa,

ndi dzanja lanu landigwera.

3 Mumnofu mwanga mulibe chamoyo chifukwa cha ukali wanu;

ndipo m’mafupa anga simuzizira, chifukwa cha cholakwa changa.

4 Pakuti mphulupulu zanga zapitirira pamutu panga;

ndathodwa nazo monga ndi katundu wolemera.

5 Mabala anga anunkha, adaola,

chifukwa cha kupusa kwanga.

6 Ndapindika, ndawerama kwakukulu;

ndimayenda woliralira tsiku lonse.

7 Pakuti m’chuuno mwanga mutentha kwambiri;

palibe pamoyo m’mnofu mwanga.

8 Ndafooka ine, ndipo ndachinjizidwa,

ndabangula chifukwa cha kumyuka mtima wanga.

9 Ambuye, chikhumbo changa chonse chili pamaso panu;

ndipo kubuula kwanga sikubisika kwa Inu.

10 Mtima wanga ugundagunda, mphamvu yanga yachoka,

ndipo kuunika kwa maso anga, ndi iko komwe kwandichokera.

11 Ondikonda ndi anzanga apewa mliri wanga;

ndipo anansi anga aima patali.

12 Ndipo anditchera misampha iwo akufuna moyo wanga;

ndipo iwo akuyesa kundichitira choipa alankhula zoononga,

nalingirira zonyenga tsiku lonse.

13 Koma ine, monga gonthi, sindimva;

ndipo monga munthu wosalankhula,

sinditsegula pakamwa panga.

14 Inde ndikunga munthu wosamva,

ndipo m’kamwa mwanga mulibe makani.

15 Pakuti ndikuyembekezani Inu, Yehova;

Inu mudzayankha, Ambuye Mulungu wanga.

16 Pakuti ndinati, Asakondwerere ine;

pakuterereka phazi langa, asadzikuze pa ine.

17 Ndafikana potsimphina,

ndipo chisoni changa chili pamaso panga chikhalire.

18 Pakuti ndidzafotokozera mphulupulu yanga;

nditenga nkhawa chifukwa cha tchimo langa.

19 Koma adani anga ali ndi moyo, nakhala ndi mphamvu,

ndipo akundida kopanda chifukwa achuluka.

20 Ndipo iwo akubwezera choipa pa chabwino

atsutsana nane, popeza nditsata chabwino.

21 Musanditaye, Yehova,

Mulungu wanga, musakhale kutali ndi ine.

22 Fulumirani kundithandiza,

Ambuye, chipulumutso changa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/38-7b3dae37b413a81d84a084883bd1d0e0.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 39

Kupepuka kwa moyo uno

Kwa Mkulu wa Nyimbo, kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

1 Ndinati, Ndidzasunga njira zanga,

kuti ndingachimwe ndi lilime langa.

Ndidzasunga pakamwa panga ndi cham’kamwa,

pokhala woipa ali pamaso panga.

2 Ndinatonthola osanena mau,

ndinakhala chete osalawa chokoma;

ndipo chisoni changa chinabuka.

3 Mtima wanga unatentha m’kati mwa ine;

unayaka moto pakulingirira ine.

Pamenepo ndinalankhula ndi lilime langa,

4 Yehova, mundidziwitse chimaliziro changa,

ndi mawerengedwe a masiku anga ndi angati;

ndidziwe malekezero anga.

5 Onani, munaika masiku anga akhale monga kuyesa dzanja;

ndipo zaka zanga zili ngati chabe pamaso panu,

Indedi munthu aliyense angakhale wokhazikika, ali chabe konse.

6 Indedi munthu ayenda ngati mthunzi;

Indedi avutika chabe: Asonkhanitsa chuma,

ndipo sadziwa adzachilandira ndani?

7 Ndipo tsopano, Ambuye, ndilindira chiyani?

Chiyembekezo changa chili pa Inu.

8 Ndipulumutseni kwa zolakwa zanga zonse,

musandiike ndikhale chotonza cha wopusa.

9 Ndinakhala duu, sindinatsegule pakamwa panga;

chifukwa inu mudachichita.

10 Mundichotsere chovutitsa chanu;

pandithera ine chifukwa cha kulanga kwa dzanja lanu.

11 Pamene mulanga munthu ndi zomdzudzula chifukwa cha mphulupulu,

mukanganula kukongola kwake monga mumachita ndi njenjete.

Indedi, munthu aliyense ali chabe.

12 Imvani pemphero langa, Yehova,

ndipo tcherani khutu kulira kwanga;

musakhale chete pa misozi yanga;

Pakuti ine ndine mlendo ndi Inu,

wosakhazikika, monga makolo anga onse.

13 Ndiloleni, kuti nditsitsimuke,

ndisanamuke ndi kukhala kuli zii.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/39-1e42e71a4b9cc5abcfdee62c5502a571.mp3?version_id=1068—