Posautsidwa Davide adandaulira, apemphera, ayamika Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Ajelet Hasakara. Salimo la Davide.
1 Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?
Mukhaliranji kutali kwa chipulumutso changa,
ndi kwa mau a kubuula kwanga?
2 Mulungu wanga, ndiitana usana, koma simuvomereza;
ndipo usiku, sindikhala chete.
3 Koma Inu ndinu woyera,
wakukhala m’malemekezo a Israele.
4 Makolo athu anakhulupirira Inu;
anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.
5 Anafuula kwa Inu, napulumutsidwa;
anakhulupirira Inu, ndipo sanachite manyazi.
6 Koma ine ndine nyongolotsi, si munthu ai,
chotonza cha anthu, ndi wonyozedwa ndi anthu.
7 Onse akundipenya andiseka;
akwenzula, apukusa mutu, nati,
8 Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa,
amlanditse tsopano popeza akondwera naye.
9 Pakuti Inu ndinu wondibadwitsa;
wondikhulupiritsa pokhala ine pa bere la mai wanga.
10 Chibadwire ine anandisiyira Inu,
kuyambira kwa mai wanga Mulungu wanga ndinu.
11 Musandikhalire kutali; pakuti nsautso ili pafupi,
pakuti palibe mthandizi.
12 Ng’ombe zamphongo zambiri zandizinga;
mphongo zolimba za ku Basani zandizungulira.
13 Andiyasamira m’kamwa mwao,
ngati mkango wozomola ndi wobangula.
14 Ndathiridwa pansi monga madzi,
ndipo mafupa anga onse anaguluka.
Mtima wanga ukunga sera;
wasungunuka m’kati mwa matumbo anga.
15 Mphamvu yanga yauma ngati phale;
ndi lilime langa likangamira kunsaya zanga;
ndipo mwandifikitsa kufumbi la imfa.
16 Pakuti andizinga agalu,
msonkhano wa oipa wanditsekereza;
andiboola m’manja anga ndi m’mapazi anga.
17 Ndikhoza kuwerenga mafupa anga onse;
iwo ayang’ana nandipenyetsetsa ine.
18 Agawana zovala zanga,
nachita maere pa malaya anga.
19 Koma Inu, Yehova, musakhale kutali;
mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.
20 Landitsani moyo wanga kulupanga;
wokondedwa wanga kumphamvu ya galu,
21 ndipulumutseni m’kamwa mwa mkango;
inde mwandiyankha ine ndili pa nyanga za njati.
22 Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga,
pakati pa msonkhano ndidzakulemekezani.
23 Inu akuopa Yehova, mumlemekeze;
inu nonse mbumba ya Yakobo, mumchitire ulemu;
ndipo muchite mantha ndi Iye, inu nonse mbumba ya Israele.
24 Pakuti sanapeputse ndipo sananyansidwe
ndi zunzo la wozunzika;
ndipo sanambisire nkhope yake;
koma pomfuulira Iye, anamva.
25 Lemekezo langa lidzakhala la Inu mu msonkhano waukulu,
zowinda zanga ndidzazichita pamaso pa iwo akumuopa Iye.
26 Ozunzika adzadya nadzakhuta,
adzayamika Yehova iwo amene amfuna,
ukhale moyo mtima wako nthawi zonse.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira
nadzatembenukira kwa Yehova,
ndipo mafuko onse aamitunduadzagwadira pamaso panu.
28 Pakuti ufumuwo ngwa Yehova;
Iye achita ufumu mwa amitundu.
29 Onenepa onse a padziko lapansi adzadya nadzagwadira;
onse akutsikira kufumbi adzawerama pamaso pake,
ndi iye amene sadziwa kusunga moyo wake.
30 Mbumba ya anthu idzamtumikira;
kudzanenedwa za Ambuye ku mibadwo yakudza.
31 Iwo adzadza nadzafotokozera chilungamo chake
kwa anthu akadzabadwa, kuti Iye anachichita.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/22-be2bc28b2bd260d5d7142d35176ffe14.mp3?version_id=1068—