Zolengedwa zonse zilemekeze Mulungu
1 Aleluya.
Lemekezani Mulungu m’malo ake oyera;
mlemekezeni m’thambo la mphamvu yake.
2 Mlemekezeni chifukwa cha ntchito zake zolimba;
mlemekezeni monga mwa ukulu wake waunjinji.
3 Mlemekezeni ndi kulira kwa lipenga;
mlemekezeni ndi chisakasa ndi zeze.
4 Mlemekezeni ndi lingaka ndi kuthira mang’ombe:
Mlemekezeni ndi zoimbira za zingwe ndi chitoliro.
5 Mlemekezeni ndi nsanje zomveka:
Mlemekezeni ndi nsanje zoliritsa.
6 Zonse zakupuma zilemekeze Yehova.
Aleluya.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/150-cc3e9fddf631e35069b3094bda171bd4.mp3?version_id=1068—