Categories
MASALIMO

MASALIMO 150

Zolengedwa zonse zilemekeze Mulungu

1 Aleluya.

Lemekezani Mulungu m’malo ake oyera;

mlemekezeni m’thambo la mphamvu yake.

2 Mlemekezeni chifukwa cha ntchito zake zolimba;

mlemekezeni monga mwa ukulu wake waunjinji.

3 Mlemekezeni ndi kulira kwa lipenga;

mlemekezeni ndi chisakasa ndi zeze.

4 Mlemekezeni ndi lingaka ndi kuthira mang’ombe:

Mlemekezeni ndi zoimbira za zingwe ndi chitoliro.

5 Mlemekezeni ndi nsanje zomveka:

Mlemekezeni ndi nsanje zoliritsa.

6 Zonse zakupuma zilemekeze Yehova.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/150-cc3e9fddf631e35069b3094bda171bd4.mp3?version_id=1068—