Categories
MASALIMO

MASALIMO 100

Olengedwa ndi Mulungu amlemekeze

Salimo la Chiyamiko.

1 Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2 Tumikirani Yehova ndi chikondwerero:

Idzani pamaso pake ndi kumuimbira mokondwera.

3 Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu;

Iyeyu anatilenga, ndipo ife ndife ake;

ndife anthu ake ndi nkhosa zapabusa pake.

4 Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko,

ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo:

Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.

5 Pakuti Yehova ndiye wabwino;

chifundo chake chimanka muyaya;

ndi chikhulupiriko chake ku mibadwomibadwo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/100-aa94a0038194128acb99efca962c0162.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 101

Davide akuti adzasamala okhulupirika nadzachotsa oipa

Salimo la Davide.

1 Ndidzaimba zachifundo ndi chiweruzo;

ndidzaimba zakukulemekezani Inu, Yehova.

2 Ndidzachita mwanzeru m’njira yangwiro;

mudzandidzera liti?

Ndidzayenda m’nyumba mwanu ndi mtima wangwiro.

3 Sindidzaika chinthu choipa pamaso panga;

chochita iwo akupatuka padera chindiipira;

sichidzandimamatira.

4 Mtima wopulukira udzandichokera;

sindidzadziwana naye woipa.

5 Wakuneneza mnzake m’tseri ndidzamdula;

wa maso odzikuza ndi mtima wodzitama sindidzamlola.

6 Maso anga ayang’ana okhulupirika m’dziko, kuti akhale ndi Ine;

iye amene ayenda m’njira yangwiro, iyeyu adzanditumikira Ine.

7 Wakuchita chinyengo sadzakhala m’kati mwa nyumba yanga;

wakunena mabodza sadzakhazikika pamaso panga.

8 Mamawa onse ndidzadula oipa onse a m’dziko;

kuduliratu onse akuchita zopanda pake kumzinda wa Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/101-c79d9d75fa245d4b3f9ed3cd86427ff4.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 102

Wopsinjika apempha Mulungu achitire anthu ake chifundo, amitundu nammverenso

Pemphero la Wozunzika, m’mene anakomoka natsanulira cholingalira chake pamaso pa Yehova.

1 Yehova, imvani pemphero langa,

ndipo mfuu wanga ufikire Inu.

2 Musandibisire nkhope yanu tsiku la nsautso yanga;

munditchereze khutu lanu;

tsiku limene ndiitana ine mundiyankhe msanga.

3 Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi,

ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.

4 Mtima wanga ukunga udzu womweta, nufota;

popeza ndiiwala kudya mkate wanga.

5 Chifukwa cha liu la kubuula kwanga

mnofu wanga umamatika kumafupa anga.

6 Ndikunga vuwo m’chipululu;

ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.

7 Ndidikira, ndikhala ngati mbalame

ili yokha pamwamba pa tsindwi.

8 Adani anga anditonza tsiku lonse;

akundiyalukirawo alumbirira ine.

9 Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate,

ndi kusakaniza chomwera changa ndi misozi,

10 chifukwa cha ukali wanu ndi kuzaza kwanu;

popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.

11 Masiku anga akunga mthunzi womka m’tali;

ndipo ine ndauma ngati udzu.

12 Koma Inu, Yehova, mukhalabe kunthawi yonse;

ndi chikumbukiro chanu ku mibadwomibadwo.

13 Inu mudzauka, ndi kuchitira nsoniZiyoni;

popeza yafika nyengo yakumchitira chifundo, nyengo yoikika.

14 Pakuti atumiki anu akondwera nayo miyala yake,

nachitira chifundo fumbi lake.

15 Pamenepoamitunduadzaopa dzina la Yehova,

ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu.

16 Pakuti Yehova anamanga Ziyoni,

anaoneka mu ulemerero wake;

17 anasamalira pemphero la iwo akusowa konse,

osapepula pemphero lao.

18 Ichi adzachilembera mbadwo ukudza;

ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.

19 Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ake opatulika;

Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;

20 kuti amve kubuula kwa wandende;

namasule ana a imfa.

21 Kuti anthu alalikire dzina la Yehova mu Ziyoni,

ndi chilemekezo chake muYerusalemu;

22 Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu,

ndi maufumu kuti atumikire Yehova.

23 Iye analanda mphamvu yanga panjira;

anachepsa masiku anga.

24 Ndinati, Mulungu wanga, musandichotse pakati pa masiku anga:

Zaka zanu zikhalira m’mibadwomibadwo.

25 Munakhazika dziko lapansi kalelo;

ndipo zakumwamba ndizo ntchito ya manja anu.

26 Zidzatha izi, koma Inu mukhala:

Inde, zidzatha zonse ngati chovala;

mudzazisintha ngati malaya, ndipo zidzasinthika:

27 Koma Inu ndinu yemweyo,

ndi zaka zanu sizifikira kutha.

28 Ana a atumiki anu adzakhalitsa,

ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/102-49465b440a1a1f3bc67c9b0b36b64c7c.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 103

Alemekeze Yehova pa chifundo chake chachikulu

Salimo la Davide.

1 Lemekeza Yehova, moyo wanga;

ndi zonse za m’kati mwanga zilemekeze dzina lake loyera.

2 Lemekeza Yehova, moyo wanga,

ndi kusaiwala zokoma zake zonse atichitirazi:

3 Amene akhululukira mphulupulu zako zonse;

nachiritsa nthenda zako zonse;

4 amene aombola moyo wako ungaonongeke;

nakuveka korona wa chifundo ndi nsoni zokoma:

5 Amene akhutitsa m’kamwa mwako ndi zabwino;

nabweza ubwana wako unge mphungu.

6 Yehova achitira onse osautsidwa

chilungamo ndi chiweruzo.

7 Analangiza Mose njira zake,

ndi ana a Israele machitidwe ake.

8 Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wachisomo,

wosakwiya msanga, ndi wa chifundo chochuluka.

9 Sadzatsutsana nao nthawi zonse;

ndipo sadzasunga mkwiyo wake kosatha.

10 Sanatichitira monga mwa zolakwa zathu,

kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.

11 Pakuti monga m’mwamba mutalikira ndi dziko lapansi,

motero chifundo chake chikulira iwo akumuopa Iye.

12 Monga kum’mawa kutanimpha ndi kumadzulo,

momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.

13 Monga atate achitira ana ake chifundo,

Yehova achitira chifundo iwo akumuopa Iye.

14 Popeza adziwa mapangidwe athu;

akumbukira kuti ife ndife fumbi.

15 Koma munthu, masiku ake akunga udzu;

aphuka monga duwa lakuthengo.

16 Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe:

Ndi malo ake salidziwanso.

17 Koma chifundo cha Yehova ndicho choyambira nthawi yosayamba

kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye,

ndi chilungamo chake kufikira kwa ana a ana;

18 kwa iwo akusungachipanganochake,

ndi kwa iwo akukumbukira malangizo ake kuwachita.

19 Yehova anakhazika mpando wachifumu wake Kumwamba;

ndi ufumu wake uchita mphamvu ponsepo.

20 Lemekezani Yehova, inuangeloake;

a mphamvu zolimba, akuchita mau ake,

akumvera liu la mau ake.

21 Lemekezani Yehova, inu makamu ake onse;

inu atumiki ake akuchita chomkondweretsa Iye.

22 Lemekezani Yehova, inu, ntchito zake zonse,

ponseponse pali ufumu wake:

Lemekeza Yehova, moyo wanga iwe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/103-bb77833f2fd6c75b7d2f1ad734162366.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 104

Ulemerero wa Mulungu m’zolengedwa ndi m’kuzisunga komwe

1 Lemekeza Yehova, moyo wanga;

Yehova, Mulungu wanga, Inu ndinu wamkulukulu;

2 muvala ulemu ndi chifumu.

Amene mudzikuta nako kuunika monga ndi chovala;

ndi kuyala thambo ngati nsalu yotchinga.

3 Amene alumikiza mitanda ya zipinda zake m’madzi;

naika makongwa akhale agaleta ake;

nayenda pa mapiko a mphepo.

4 Amene ayesa mphepo amithenga ake;

lawi la moto atumiki ake;

5 anakhazika dziko lapansi pa maziko ake,

silidzagwedezeka kunthawi yonse.

6 Mudalikuta ndi nyanja ngati ndi chovala;

madzi anafikira pamwamba pa mapiri.

7 Pa kudzudzula kwanu anathawa;

anathawa msanga liu la bingu lanu;

8 anakwera m’mapiri, anatsikira m’zigwa,

kufikira malo mudawakonzeratu.

9 Munaika malire kuti asapitirireko;

kuti asabwererenso kuphimba dziko lapansi.

10 Atumiza akasupe alowe m’makwawa;

ayenda pakati pa mapiri:

11 Zimamwamo nyama zonse zakuthengo;

mbidzi zipherako ludzu lao.

12 Mbalame za mlengalenga zifatsa pamenepo,

zimaimba pakati pa mitawi.

13 Iye amwetsa mapiri mochokera m’zipinda zake:

Dziko lakhuta zipatso za ntchito zanu.

14 Ameretsa msipu ziudye ng’ombe,

ndi zitsamba achite nazo munthu;

natulutse chakudya chochokera m’nthaka;

15 ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu,

ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yake,

ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu.

16 Mitengo ya Yehova yadzala ndi madzi;

mikungudza ya ku Lebanoni imene anaioka;

17 m’mwemo mbalame zimanga zisa zao;

pokhala chumba mpa mitengo ya mikungudza.

18 Mapiri aatali ndiwo ayenera zinkhoma;

pamatanthwe mpothawirapo mbira.

19 Anaika mwezi nyengo zake;

dzuwa lidziwa polowera pake.

20 Muika mdima ndipo pali usiku;

pamenepo zituluka zilombo zonse za m’thengo.

21 Misona ya mkango ibangula potsata nyama yao,

nifuna chakudya chao kwa Mulungu.

22 Potuluka dzuwa, zithawa,

zigona pansi m’ngaka mwao.

23 Pamenepo munthu atulukira kuntchito yake,

nagwiritsa kufikira madzulo.

24 Ntchito zanu zichulukadi, Yehova!

Munazichita zonse mwanzeru;

dziko lapansi lidzala nacho chuma chanu.

25 Nyanja siyo, yaikulu ndi yachitando,

m’mwemo muli zokwawa zosawerengeka;

zamoyo zazing’ono ndi zazikulu.

26 M’mwemo muyenda zombo;

ndiLeviyataniamene munamlenga aseweremo.

27 Izi zonse zikulindirirani,

muzipatse chakudya chao pa nyengo yake.

28 Chimene muzipatsa zigwira;

mufumbatula dzanja lanu, zikhuta zabwino.

29 Mukabisa nkhope yanu, ziopsedwa;

mukalanda mpweya wao, zikufa,

ndipo zibwerera kufumbi kwao.

30 Potumizira mzimu wanu, zilengedwa;

ndipo mukonzanso nkhope ya dziko lapansi.

31 Ulemerero wa Yehova ukhale kosatha;

Yehova akondwere mu ntchito zake;

32 amene apenyerera padziko lapansi, ndipo linjenjemera;

akhudza mapiri, ndipo afuka.

33 Ndidzaimbira Yehova m’moyo mwanga:

ndidzaimbira Mulungu wanga zomlemekeza pokhala ndilipo.

34 Pomlingirira Iye pandikonde;

ndidzakondwera mwa Yehova.

35 Ochimwa athedwe kudziko lapansi,

ndi oipa asakhalenso.

Yamika Yehova, moyo wanga.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/104-90ec120186134980a5e19a6a2f99ffb8.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 105

Alemekeza Yehova pa zodabwitsa adazichitira ana a Israele

1 Yamikani Yehova, itanirani pa dzina lake;

bukitsani mwa mitundu ya anthu zochita Iye.

2 Muimbireni, muimbireni zomlemekeza;

fotokozerani zodabwitsa zake zonse.

3 Mudzitamandire ndi dzina lake loyera:

mitima yao ya iwo ofunsira Yehova ikondwere.

4 Funani Yehova, ndi mphamvu yake;

funsirani nkhope yake nthawi zonse.

5 Kumbukirani zodabwitsa zake adazichita;

zizindikiro zake ndi maweruzo a pakamwa pake;

6 inu mbeu za Abrahamu, mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhika ake.

7 Iye ndiye Yehova, Mulungu wathu;

maweruzo ake akhala padziko lonse lapansi.

8 Akumbukirachipanganochake kosatha,

mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

9 chipanganocho anapangana ndi Abrahamu,

ndi lumbiro lake ndi Isaki;

10 ndipo anachiimikira Yakobo, chikhale malemba,

chikhale chipangano chosatha kwa Israele.

11 Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,

gawo la cholowa chako;

12 pokhala iwo anthu owerengeka,

inde, anthu pang’ono, ndi alendo m’mwemo;

13 nayendayenda kuchokera mtundu wina kufikira mtundu wina,

kuchokera ufumu wina kufikira anthu ena.

14 Sanalola munthu awasautse;

ndipo anadzudzula mafumu chifukwa cha iwowa.

15 Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga,

musamachitira choipa aneneri anga.

16 Ndipo anaitana njala igwere dziko;

anathyola mchirikizo wonse wa mkate.

17 Anawatsogozeratu munthu;

anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:

18 Anapweteka miyendo yake ndi matangadza;

anamgoneka mu unyolo;

19 kufikira nyengo yakuchitika maneno ake;

mau a Yehova anamuyesa.

20 Mfumuyo anatuma munthu nammasula;

woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira.

21 Anamuika akhale woyang’anira nyumba yake,

ndi woweruza wa pa zake zonse:

22 Amange nduna zake iye mwini,

alangize akulu ake adziwe nzeru.

23 Pamenepo Israele analowa mu Ejipito;

ndi Yakobo anakhala mlendo m’dziko la Hamu.

24 Ndipo anachulukitsatu mtundu wa anthu ake,

nawapatsa mphamvu yoposa owasautsa.

25 Anasanduliza mitima yao, kuti adane nao anthu ake,

kuti achite monyenga ndi atumiki ake.

26 Anatuma Mose mtumiki wake,

ndi Aroni amene adamsankha.

27 Anaika pakati pao zizindikiro zake,

ndi zodabwitsa m’dziko la Hamu.

28 Anatumiza mdima ndipo kunada;

ndipo sanapikisane nao mau ake.

29 Anasanduliza madzi ao akhale mwazi,

naphanso nsomba zao.

30 Dziko lao linachuluka achule,

m’zipinda zomwe za mafumu ao.

31 Ananena, ndipo inadza mitambo ya ntchentche,

ndi nsabwe kufikira m’malire ao onse.

32 Anawapatsa mvula yamatalala,

lawi la moto m’dziko lao.

33 Ndipo anapanda mipesa yao, ndi mikuyu yao;

nathyola mitengo kufikira m’malire ao onse.

34 Ananena, ndipo linadza dzombe

ndi mphuchi, ndizo zosawerengeka,

35 ndipo zinadya zitsamba zonse za m’dziko mwao,

zinadyanso zipatso za m’nthaka mwao.

36 Ndipo Iye anapha achisamba onse m’dziko mwao,

choyambira cha mphamvu yao yonse.

37 Ndipo anawatulutsa pamodzi ndisilivandi golide:

ndi mwa mafuko ao munalibe mmodzi wokhumudwa.

38 Ejipito anakondwera pakuchoka iwo;

popeza kuopsa kwao kudawagwera.

39 Anayala mtambo uwaphimbe;

ndi moto uunikire usiku.

40 Anafunsa ndipo Iye anadzetsa zinziri,

nawakhutitsa mkate wakumwamba.

41 Anatsegula pathanthwe, anatulukamo madzi;

nayenda pouma ngati mtsinje.

42 Popeza anakumbukira mau ake oyera,

ndi Abrahamu mtumiki wake.

43 Potero anatulutsa anthu ake ndi kusekerera,

osankhika ake ndi kufuula mokondwera.

44 Ndipo anawapatsa maiko aamitundu;

iwo ndipo analanda zipatso za ntchito ya anthu:

45 Kuti asamalire malemba ake,

nasunge malamulo ake.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/105-1a121a1b6be5a64d57ca46db97f36064.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 106

Israele anapikisana ndi Yehova kwambiri, Iye nawalanga nawalanditsanso. Amlemekezepo

1 Aleluya.

Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino:

Pakuti chifundo chake nchosatha.

2 Adzafotokoza ndani ntchito zamphamvu za Yehova,

adzamveketsa ndani chilemekezo chake chonse?

3 Odala iwo amene asunga chiweruzo,

iye amene achita chilungamo nthawi zonse.

4 Mundikumbukire, Yehova,

monga momwe muvomerezana ndi anthu anu;

mundionetsa chipulumutso chanu:

5 Kuti ndione chokomacho cha osankhika anu,

kuti ndikondwere nacho chikondwerero cha anthu anu,

kuti ndidzitamandire pamodzi ndi cholowa chanu.

6 Talakwa pamodzi ndi makolo athu;

tachita mphulupulu, tachita choipa.

7 Makolo athu sanadziwitse zodabwitsa zanu mu Ejipito;

sanakumbukire zachifundo zanu zaunyinji;

koma anapikisana ndi Inu kunyanja, ku Nyanja Yofiira.

8 Koma anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake,

kuti adziwitse chimphamvu chake.

9 Ndipo anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inaphwa:

Potero anawayendetsa mozama ngati m’chipululu.

10 Ndipo anawapulumutsa m’dzanja la iye amene anawada,

nawaombola kudzanja la mdani.

11 Ndipo madziwo anamiza owasautsa;

sanatsale mmodzi yense.

12 Pamenepo anavomereza mau ake;

anaimbira chomlemekeza.

13 Koma anaiwala ntchito zake msanga;

sanalindire uphungu wake:

14 Popeza analakalakatu kuchidikhako,

nayesa Mulungu m’chipululu.

15 Ndipo anawapatsa chopempha iwo;

koma anaondetsa mitima yao.

16 Ndipo kumisasa anachita nao nsanje Mose

ndi Aroni woyerayo wa Yehova.

17 Dziko lidayasama nilidameza Datani,

ndipo linafotsera gulu la Abiramu.

18 Ndipo m’gulu mwao mudayaka moto;

lawi lake lidapsereza oipawo.

19 Anapanga mwanawang’ombe ku Horebu,

nagwadira fano loyenga.

20 M’mwemo anasintha ulemerero wao

ndi fanizo la ng’ombe yakudya msipu.

21 Anaiwala Mulungu Mpulumutsi wao,

amene anachita zazikulu mu Ejipito;

22 zodabwitsa m’dziko la Hamu,

zoopsa ku Nyanja Yofiira.

23 Potero Iye adati awaononge,

pakadapanda Mose wosankhika wake,

kuima pamaso pake pogamukapo,

kubweza ukali wake ungawaononge.

24 Anapeputsanso dziko lofunika,

osavomereza mau ake;

25 koma anadandaula m’mahema mwao,

osamvera mau a Yehova.

26 Potero anawasamulira dzanja lake,

kuti awagwetse m’chipululu:

27 Kugwetsanso mbeu zao mwaamitundu,

ndi kuwabalalitsa m’maiko maiko.

28 Ndipo anadziphatikiza ndi Baala-Peori,

nadyanso nsembe za akufa.

29 Ndipo anamkwiyitsa nazo zochita zao;

kotero kuti mliri unawagwera.

30 Pamenepo panauka Finehasi, nachita chilango:

Ndi mliriwo unaletseka.

31 Ndipo adamuyesa iye wachilungamo,

ku mibadwomibadwo kunthawi zonse.

32 Anautsanso mkwiyo wake kumadzi a Meriba,

ndipo kudaipira Mose chifukwa cha iwowa:

33 Pakuti anawawitsa mzimu wake,

ndipo analankhula zosayenera ndi milomo yake.

34 Sanaononga mitunduyo ya anthu,

imene Yehova adawauza;

35 koma anasokonekerana nao amitundu,

naphunzira ntchito zao:

36 Ndipo anatumikira mafano ao,

amene anawakhalira msampha:

37 Ndipo anapereka ana ao aamuna ndi aakazi nsembe ya kwa ziwanda,

38 nakhetsa mwazi wosachimwa,

ndiwo mwazi wa ana ao aamuna ndi aakazi,

amene anawaperekera nsembe mafano a Kanani;

m’mwemo analidetsa dziko ndi mwaziwo.

39 Ndipo anadziipsa nazo ntchito zao,

nachita chigololo nao machitidwe ao.

40 Potero udayaka mkwiyo wa Yehova pa anthu ake,

nanyansidwa Iye ndi cholowa chake.

41 Ndipo anawapereka m’manja a amitundu;

ndipo odana nao anachita ufumu pa iwo.

42 Adani ao anawasautsanso,

nawagonjetsa agwire mwendo wao.

43 Iye anawalanditsa kawirikawiri;

koma anapikisana ndi Iye mwa uphungu wao,

ndi mphulupulu zao zinawafoketsa.

44 Koma anapenya nsautso yao,

pakumva kufuula kwao:

45 Ndipo anawakumbukirachipanganochake,

naleza monga mwa kuchuluka kwa chifundo chake.

46 Ndipo anawachitira kuti apeze nsoni

pamaso pa onse amene adawamanga ndende.

47 Tipulumutseni, Yehova, Mulungu wathu,

ndi kutisokolotsa kwa amitundu,

kuti tiyamike dzina lanu loyera,

ndi kudzitamandira nacho chilemekezo chanu.

48 Wodala Yehova, Mulungu wa Israele,

kuyambira kosayamba kufikira kosatha.

Ndi anthu onse anene,Amen.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/106-38135923c8802db246d8450c9533e008.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 107

Olanditsidwa, alendo, omangidwa, odwala, amalinyero ndi ena onse alemekeze Yehova

1 Yamikani Yehova pakuti Iye ndiye wabwino;

pakuti chifundo chake nchosatha.

2 Atere oomboledwa a Yehova,

amene anawaombola m’dzanja la wosautsa;

3 nawasokolotsa kumaiko,

kuchokera kum’mawa ndi kumadzulo,

kumpoto ndi kunyanja.

4 Anasokera m’chipululu, m’njira yopanda anthu;

osapeza mzinda wokhalamo.

5 Anamva njala ndi ludzu,

moyo wao unakomoka m’kati mwao.

6 Pamenepo anafuulira kwa Yehova mumsauko mwao,

ndipo anawalanditsa m’kupsinjika kwao.

7 Ndipo anawatsogolera panjira yolunjika,

kuti amuke kumzinda wokhalamo.

8 Ayamike Yehova chifukwa cha chifundo chake,

ndi zodabwitsa zake za kwa ana a anthu!

9 Pakuti akhutitsa mtima wolakalaka,

nadzaza mtima wanjala ndi zabwino.

10 Iwo akukhala mumdima ndi mu mthunzi wa imfa,

omangika ndi kuzunzika ndi chitsulo;

11 popeza anapikisana nao mau a Mulungu,

napeputsa uphungu wa Wam’mwambamwamba;

12 kotero kuti anagonjetsa mtima wao ndi chovuta;

iwowa anakhumudwa koma panalibe mthandizi.

13 Pamenepo anafuulira kwa Yehova mumsauko mwao,

ndipo anawapulumutsa m’kupsinjika kwao.

14 Anawatulutsa mumdima ndi mu mthunzi wa imfa,

nadula zomangira zao.

15 Ayamike Yehova chifukwa cha chifundo chake,

ndi zodabwitsa zake za kwa ana a anthu!

16 Popeza adaswa zitseko zamkuwa,

nathyola mipiringidzo yachitsulo.

17 Anthu opusa azunzika chifukwa cha zolakwa zao,

ndi chifukwa cha mphulupulu zao.

18 Mtima wao unyansidwa nacho chakudya chilichonse;

ndipo ayandikira zipata za imfa.

19 Pamenepo afuulira kwa Yehova m’kusauka kwao,

ndipo awapulumutsa m’kupsinjika kwao.

20 Atumiza mau ake nawachiritsa,

nawapulumutsa ku chionongeko chao.

21 Ayamike Yehova chifukwa cha chifundo chake,

ndi zodabwitsa zake za kwa ana a anthu!

22 Ndipo apereke nsembe zachiyamiko,

nafotokozere ntchito zake ndi kufuula mokondwera.

23 Iwo akutsikira kunyanja nalowa m’zombo,

akuchita ntchito zao pamadzi aakulu.

24 Iwowa apenya ntchito za Yehova,

ndi zodabwitsa zake m’madzi ozama.

25 Popeza anena, nautsa namondwe,

amene autsa mafunde ake.

26 Akwera kuthambo, atsikira kozama;

mtima wao usungunuka nacho choipacho.

27 Adzandira napambanitsa miyendo ngati munthu woledzera,

nathedwa nzeru konse.

28 Pamenepo afuulira kwa Yehova m’kusauka kwao,

ndipo awatulutsa m’kupsinjika kwao.

29 Asanduliza namondwe akhale bata,

kotero kuti mafunde ake atonthole.

30 Pamenepo akondwera, popeza pagwa bata;

ndipo Iye awatsogolera kudooko afunako.

31 Ayamike Yehova chifukwa cha chifundo chake,

ndi zodabwitsa zake za kwa ana a anthu!

32 Amkwezenso mu msonkhano wa anthu,

namlemekeze pokhala akulu.

33 Asanduliza mitsinje ikhale chipululu,

ndi akasupe a madzi akhale nthaka youma.

34 Dziko la zipatso, likhale lakhulo,

chifukwa cha choipa cha iwo okhalamo.

35 Asanduliza chipululu chikhale thawale,

ndi dziko louma likhale akasupe a madzi.

36 Ndi apo akhalitsa anjala,

kuti amangeko mzinda wokhalamo anthu;

37 nafese m’minda, naoke mipesa,

ndiyo yakubala zipatso zambiri.

38 Ndipo awadalitsa, kotero kuti achuluka kwambiri;

osachepsanso zoweta zao.

39 Koma achepanso, nawerama,

chifukwa cha chisautso, choipa ndi chisoni.

40 Atsanulira chimpepulo pa akulu,

nawasokeretsa m’chipululu mopanda njira.

41 Koma aika waumphawi pamsanje posazunzika,

nampatsa mabanja ngati gulu la nkhosa.

42 Oongoka mtima adzachiona nadzasekera;

koma chosalungama chonse chitseka pakamwa pake.

43 Wokhala nazo nzeru asamalire izi,

ndipo azindikire zachifundo za Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/107-c55deac6f7b308043773ea8648e7aa75.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 108

Davide aimbira Mulungu womgonjetsera adani

Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Wakhazikika mtima wanga, Mulungu;

ndidzaimba, inde ndidzaimba zolemekeza, ndiko ulemerero wanga.

2 Galamukani, chisakasa ndi zeze;

ndidzauka ndekha mamawa.

3 Ndidzakuyamikani mwa mitundu ya anthu, Yehova:

ndipo ndidzaimba zakukulemekezani mwa anthu.

4 Pakuti chifundo chanu nchachikulu kupitirira kumwamba,

ndi choonadi chanu kufikira mitambo.

5 Kwezekani pamwamba pa thambo, Mulungu;

ndi ulemerero wanu pamwamba padziko lonse lapansi,

6 kuti okondedwa anu alanditsidwe,

pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja ndipo mutivomereze.

7 Mulungu analankhula m’chiyero chake; ndidzakondwerera:

ndidzagawa Sekemu; ndidzayesa muyeso chigwa cha Sukoti.

8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanga;

ndi Efuremu ndiye mphamvu ya mutu wanga;

Yuda ndiye wolamulira wanga.

9 Mowabu ndiye mkhate wanga;

pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga;

ndidzafuulira Filistiya.

10 Adzandifikitsa ndani m’mzinda wa m’linga?

Adzanditsogolera ndani ku Edomu?

11 Si ndinu Mulungu, amene mwatitaya

osatuluka nao magulu athu?

12 Tithandizeni mumsauko;

pakuti chipulumutso cha munthu ndi chabe.

13 Mwa Mulungu tidzachita molimbika mtima:

Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/108-b23f6266034aa4eada30b38fe6a206bb.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 109

Davide apempha Mulungu alange oipa, amlanditse m’manja mwao

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la Davide.

1 Mulungu wa chilemekezo changa, musakhale chete;

2 pakuti pakamwa pa woipa ndi pakamwa pa chinyengo pananditsegukira;

anandilankhulira ndi m’kamwa mwa bodza.

3 Ndipo anandizinga ndi mau a udani,

nalimbana nane kopanda chifukwa.

4 M’malo mwa chikondi changa andibwezera udani;

koma ine, kupemphera ndiko.

5 Ndipo anandisenza choipa m’malo mwa chokoma,

ndi udani m’malo mwa chikondi changa.

6 Muike munthu woipa akhale mkulu wake;

ndi mdani aime padzanja lamanja lake.

7 Ponenedwa mlandu wake atuluke wotsutsika;

ndi pemphero lake likhale ngati kuchimwa.

8 Masiku ake akhale owerengeka;

wina alandire udindo wake.

9 Ana ake akhale amasiye,

ndi mkazi wake wamasiye.

10 Ana ake akhale amchirakuyenda ndi opemphapempha;

afunefune zosowa zao kuchokera m’mabwinja mwao.

11 Wokongoletsa agwire zonse ali nazo;

ndi alendo alande za ntchito yake.

12 Pasakhale munthu wakumchitira chifundo;

kapena kuchitira chokoma ana ake amasiye.

13 Zidzukulu zake zidulidwe;

dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.

14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukike ndi Yehova;

ndi tchimo la mai wake lisafafanizidwe.

15 Zikhale pamaso pa Yehova chikhalire,

kuti adule chikumbukiro chao kuchichotsera kudziko lapansi.

16 Chifukwa kuti sanakumbukire kuchita chifundo,

koma analondola wozunzika ndi waumphawi,

ndi wosweka mtima, kuti awaphe.

17 Inde, anakonda kutemberera, ndipo kudamdzera mwini;

sanakondwere nako kudalitsa, ndipo kudamkhalira kutali.

18 Anavalanso temberero ngati malaya,

ndipo lidamlowa m’kati mwake ngati madzi,

ndi ngati mafuta m’mafupa ake.

19 Limkhalire ngati chovala adzikuta nacho,

ndi lamba limene adzimangirira nalo m’chuuno chimangirire.

20 Ichi chikhale mphotho ya otsutsana nane yowapatsa Yehova,

ndi ya iwo akunenera choipa moyo wanga.

21 Koma Inu, Yehova Ambuye,

muchite nane chifukwa cha dzina lanu;

ndilanditseni popeza chifundo chanu ndi chabwino.

22 Pakuti ine ndine wozunzika ndi waumphawi,

ndi mtima wanga walaswa m’kati mwanga.

23 Ndamuka ngati mthunzi womka m’tali;

ndiingidwa kwina ndi kwina ngati dzombe.

24 Mabondo anga agwedezeka chifukwa cha kusala;

ndi mnofu wanga waonda posowa mafuta.

25 Ndiwakhaliranso chotonza;

pakundiona apukusa mutu.

26 Ndithandizeni Yehova, Mulungu wanga:

Ndipulumutseni monga mwa chifundo chanu;

27 kuti adziwe kuti ichi ndi dzanja lanu;

kuti Inu Yehova munachichita.

28 Atemberere iwowa, koma mudalitse ndinu;

pakuuka iwowa adzachita manyazi,

koma mtumiki wanu adzakondwera.

29 Otsutsana nane avale manyazi,

nadzikute nacho chisokonezo chao ngati ndi chofunda.

30 Ndidzayamika Yehova kwakukulu pakamwa panga;

ndi pakati pa anthu aunyinji ndidzamlemekeza.

31 Popeza adzaima padzanja lamanja la waumphawi,

kumpulumutsa kwa iwo akuweruza koipa moyo wake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/109-645311000c9cff2c61ddadeadf15563b.mp3?version_id=1068—