Categories
MARKO

MARKO 10

Asasiyane mwamuna ndi mkazi wake

1 Ndipo ananyamuka Iye kumeneko, nadza ku maiko a ku Yudeya ndi ku tsidya lija la Yordani; ndipo anasonkhananso kwa Iye makamu a anthu; ndipo monga anazolowera, anawaphunzitsanso.

2 Ndipo anadza kwa IyeAfarisi, namfunsa Iye ngati kuloledwa kuti munthu achotse mkazi wake, namuyesa Iye.

3 Ndipo Iye anayankha nati kwa iwo, Kodi Mose anakulamulani chiyani?

4 Ndipo anati, Mose analola kulembera kalata yachilekaniro, ndi kumchotsa.

5 Koma Yesu anati kwa iwo, Chifukwa cha kuuma kwa mitima yanu anakulemberani lamulo ili.

6 Koma kuyambira pa chiyambi cha malengedwe anawapanga mwamuna ndi mkazi.

7 Chifukwa chake mwamuna adzasiya atate wake ndi amai wake, ndipo adzaphatikizana ndi mkazi wake;

8 ndipo awiriwa adzakhala thupi limodzi: kotero kuti salinso awiri, koma thupi limodzi.

9 Chifukwa chake chimene Mulungu anachimanga pamodzi, asachilekanitse munthu.

10 Ndipo m’nyumbaophunziraanamfunsanso za chinthu ichi.

11 Ndipo Iye ananena nao, Munthu aliyense akachotsa mkazi wake, nakakwatira wina, achita chigololo kulakwira mkaziyo;

12 ndipo ngati mkazi akachotsa mwamuna wake, nakwatiwa ndi wina, achita chigololo iyeyu.

Yesu adalitsa tiana

13 Ndipo analinkudza nato kwa Iye tiana, kuti akatikhudze; ndipo ophunzirawo anawadzudzula.

14 Koma pamene Yesu anaona anakwiya, ndipo anati kwa iwo, Lolani tiana tidze kwa Ine; musatiletse: pakuti Ufumu wa Mulungu uli wa totere.

15 Ndithu ndinena ndi inu, Munthu aliyense wosalandira Ufumu wa Mulungu ngati kamwana, sadzalowamo konse.

16 Ndipo Iye anatiyangata, natidalitsa, ndi kuika manja ake pa ito.

Mnyamata mwini chuma chambiri

17 Ndipo pamene Iye anatuluka kutsata njira, anamthamangira munthu, namgwadira Iye, namfunsa, Mphunzitsi wabwino, ndidzachita chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?

18 Ndipo Yesu anati kwa iye, Unditcha Ine wabwino bwanji? Palibe wabwino koma mmodzi, ndiye Mulungu.

19 Udziwa malamulo: Usaphe, Usachite chigololo, Usabe, Usachite umboni wakunama, Usanyenge, Lemekeza atate wako ndi amai ako.

20 Ndipo iye anati kwa Iye, Mphunzitsi, zonsezi ndinazisunga kuyambira ndili mwana.

21 Ndipo Yesu anamyang’ana, namkonda, nati kwa iye, Chinthu chimodzi chikusowa: pita, gulitsa zonse uli nazo, nuzipereke kwa anthu aumphawi, ndipo chuma udzakhala nacho m’mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

22 Koma nkhope yake inagwa pa mau awa, ndipo anachoka iye wachisoni; pakuti anali mwini chuma chambiri.

23 Ndipo Yesu anaunguzaunguza, nanena ndi ophunzira ake, Okhala nacho chuma adzalowa mu Ufumu wa Mulungu ndi kuvuta nanga!

24 Ndipo ophunzirawo anazizwa ndithu ndi mau ake. Koma Yesu anayankhanso nanena nao, Ananu, nkovuta ndithu kwa iwo akutama chuma kulowa mu Ufumu wa Mulungu!

25 Nkwa pafupi kutingamiraipyole diso la singano kuposa kuti mwini chuma alowe mu Ufumu wa Mulungu.

26 Ndipo anadabwa, nanena kwa Iye, Ndipo angathe kupulumuka ndani?

27 Yesu anawayang’ana iwo nati, Sikutheka ndi anthu, koma kutheka ndi Mulungu; pakuti zinthu zonse zitheka ndi Mulungu.

28 Petro anayamba kunena naye, Onani, ife tinasiya zonse, ndipo tinakutsatani Inu.

29 Yesu anati, Ndithu ndinena ndi inu, Palibe munthu anasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena amai, kapena atate, kapena ana, kapena minda, chifukwa cha Ine, ndi chifukwa cha Uthenga Wabwinowo,

30 amene sadzalandira makumi khumi tsopano nthawi ino, nyumba, ndi abale, ndi alongo, ndi amai, ndi ana, ndi minda, pamodzi ndi mazunzo; ndipo nthawi ilinkudza, moyo wosatha.

31 Koma ambiri akuyamba adzakhala akuthungo, ndi akuthungo adzakhala oyamba.

Ali panjira kukwera ku Yerusalemu

32 Ndipo iwo anali m’njira alinkukwera kunka ku Yerusalemu; ndipo Yesu analikuwatsogolera; ndipo iwo anazizwa; ndipo akumtsatawo anachita mantha. Ndipo Iye anatenganso khumi ndi awiriwo, nayamba kuwauza zinthu zimene zidzamfikira Iye,

33 nati, Taonani, tikwera ku Yerusalemu; ndipoMwana wa Munthuadzaperekedwa kwa ansembe aakulu ndi alembi; ndipo iwo adzamweruza kuti ayenera imfa, nadzampereka Iye kwa anthu a mitundu;

34 ndipo adzamnyoza Iye, nadzamthira malovu, nadzamkwapula Iye, nadzamupha; ndipo pofika masiku atatu adzauka.

Ana a Zebedeo apempha ulemu

35 Ndipo anadza kwa Iye Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedeo, nanena naye, Mphunzitsi, tifuna kuti mudzatichitire chimene chilichonse tidzapempha kwa Inu.

36 Ndipo Iye anati kwa iwo, Mufuna kuti ndidzakuchitireni inu chiyani?

37 Ndipo iwo anati kwa Iye, Mutipatse ife kuti tikhale mmodzi kudzanja lanu lamanja, ndi wina kulamanzere, mu ulemerero wanu.

38 Koma Yesu anati kwa iwo, Simudziwa chimene muchipempha. Mukhoza kodi kumwera chikho chimene ndimwera Ine? Kapena kubatizidwa ndi ubatizo umene ndibatizidwa nao Ine?

39 Ndipo anati kwa Iye, Tikhoza. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Chikho chimene ndimwera Ine mudzamwera; ndipo ubatizo umene ndibatizidwa nao Ine, mudzabatizidwa nao;

40 koma kukhala kudzanja langa lamanja, kapena lamanzere sikuli kwanga kupatsa; koma kuli kwa iwo amene adawakonzeratu.

41 Ndipo pamene khumiwo anamva, anayamba kupsa mtima chifukwa cha Yakobo ndi Yohane.

42 Ndipo Yesu anawaitana, nanena nao, Mudziwa kuti iwo amene ayesedwa ambuye a mitundu ya anthu amachita ufumu pa iwo; ndipo akulu ao amachita ulamuliro pa iwo.

43 Koma mwa inu sikutero ai; koma aliyense amene afuna kukhala wamkulu mwa inu adzakhala mtumiki wanu;

44 ndipo aliyense amene afuna kukhala woyamba mwa inu adzakhala kapolo wa onse.

45 Pakuti ndithu, Mwana wa Munthu sanadze kutumikiridwa, koma kutumikira, ndi kupereka moyo wake dipo la kwa anthu ambiri.

Baratimeo wakhungu wa ku Yeriko

46 Ndipo iwo anafika ku Yeriko; ndipo m’mene Iye analikutuluka mu Yeriko, ndi ophunzira ake, ndi khamu lalikulu la anthu, mwana wa Timeo, Baratimeo, wopempha wakhungu, analikukhala pansi m’mbali mwa njira.

47 Ndipo pamene anamva kuti ndi Yesu wa ku Nazarete, anayamba kufuula, ndi kunena, Yesu, Inu Mwana wa Davide, mundichitire ine chifundo.

48 Ndipo ambiri anamulamula kuti atonthole: koma makamaka anafuulitsa kuti, Inu mwana wa Davide, mundichitire chifundo.

49 Ndipo Yesu anaima, nati, Mwitaneni. Ndipo anaitana wakhunguyo, nanena naye, Limba mtima; nyamuka, akuitana.

50 Ndipo iye anataya chofunda chake, nazunzuka, nadza kwa Yesu.

51 Ndipo Yesu anamyankha, nati, Ufuna kuti ndikuchitire chiyani? Ndipo wakhunguyo anati kwa Iye, Raboni, ndilandire kuona kwanga.

52 Ndipo Yesu anati kwa iye, Muka; chikhulupiriro chako chakupulumutsa iwe. Ndipo pomwepo anapenyanso; namtsata Iye panjira.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/10-a5891fb89c35a2ecb07d1b3d2cd846cf.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 11

Yesu alowa mu Yerusalemu alikukhala pabulu

1 Ndipo pamene iwo anayandikira kuYerusalemu, ku Betefage ndi Betaniya, paphiri la Azitona, anatuma awiri aophunziraake,

2 nanena nao, Mukani, lowani m’mudzi wapandunji ndi inu; ndipo pomwepo pakulowamo mudzapeza mwana wa bulu womangidwa, amene palibe munthu anakhalapo kale lonse; mmasuleni, ndipo mubwere naye.

3 Ndipo munthu akati kwa inu, Mutero bwanji? Katini, Ambuye amfuna iye; ndipo pomwepo adzamtumiza kuno.

4 Ndipo anachoka, napeza mwana wa bulu womangidwa pakhomo, pabwalo m’khwalala, nammasula iye.

5 Ndipo ena akuima kumeneko ananena nao, Muchita chiyani ndi kumasula mwana wa bulu?

6 Ndipo anati kwa iwo monga momwe ananena Yesu: ndipo anawalola iwo apite naye.

7 Ndipo anabwera naye mwana wa bulu kwa Yesu, naika zovala zao pa iye, ndipo Iye anakhala pamenepo.

8 Ndimo ambiri anayala zovala zao panjira; ndi ena zitsamba, anazidula m’minda.

9 Ndipo akutsogolera, ndi iwo akutsata, anafuula, Hosana; Wolemekezeka Iye wakudza m’dzina la Ambuye:

10 Wolemekezeka Ufumu ulinkudza, wa atate wathu Davide; Hosana mu Kumwambamwamba.

11 Ndipo Iye analowa mu Yerusalemu, mu Kachisi; ndipo m’mene anaunguza zinthu zonse, popeza ndi madzulo, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.

Yesu atemberera mkuyu

12 Ndipo m’mawa mwake, atatuluka ku Betaniya, Iye anamva njala.

13 Ndipo anaona mkuyu kutali, uli ndi masamba; ndipo anadza Iye, kuti kapena akapezapo kanthu: ndipo m’mene anafikako anapeza palibe kanthu koma masamba okha; pakuti siinali nyengo yake ya nkhuyu.

14 Ndipo anayankha nanena ndi uwo, Munthu sadzadyanso zipatso zako nthawi zonse. Ndipo ophunzira ake anamva.

Yesu atulutsa amalonda mu Kachisi

15 Ndipo anafika iwo ku Yerusalemu; ndipo Iye analowa mu Kachisi, nayamba kutulutsa akugulitsa ndi akugula malonda mu Kachisimo, nagubuduza magome a osinthana ndalama, ndi mipando ya ogulitsa nkhunda;

16 ndipo sanalole munthu aliyense kunyamula chotengera kupyola pakati pa Kachisi.

17 Ndipo anaphunzitsa, nanena nao, Sichilembedwa kodi, Nyumba yanga idzatchedwa nyumba yakupempheramo anthu a mitundu yonse? Koma inu mwaiyesa phanga la achifwamba.

18 Ndipo ansembe aakulu ndi alembi anamva, nafunafuna momuonongera Iye; pakuti anamuopa, chifukwa khamu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.

19 Ndipo masiku onse madzulo anatuluka Iye m’mzinda.

Mkuyu wouma

20 Ndipo m’mene anapitapo m’mawa mwake, anaona kuti mkuyu uja unafota, kuyambira kumizu.

21 Ndipo Petro anakumbukira, nanena naye,Rabi, onani, wafota mkuyuwo munautemberera.

22 Ndipo Yesu anayankha nanena nao, Khulupirirani Mulungu.

23 Ndithu ndinena ndi inu, kuti, Munthu aliyense akanena ndi phiri ili, Tanyamulidwa, nuponyedwe m’nyanja; wosakayika mumtima mwake, koma adzakhulupirira kuti chimene achinena chichitidwa, adzakhala nacho.

24 Chifukwa chake ndinena ndi inu, Zinthu zilizonse mukazipemphera ndi kuzipempha, khulupirirani kuti mwazilandira, ndipo mudzakhala nazo.

25 Ndipo pamene muimirira ndi kupemphera, khululukirani, ngati munthu wakulakwirani kanthu; kuti Atate wanunso ali Kumwamba akhululukire inu zolakwa zanu.

Ubatizo wa Yohane

27 Ndipo iwo anadzanso ku Yerusalemu; ndipo m’mene Iye anali kuyenda mu Kachisi, anafika kwa Iye ansembe aakulu, ndi alembi ndi akulu;

28 nanena naye, Izi muzichita ndi ulamuliro wotani? Kapena anakupatsani ndani ulamuliro uwu wakuchita izi?

29 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ndikufunsani mau amodzi, mundiyankhe Ine, ndipo ndidzakuuzani ulamuliro umene ndichita nao zinthu zimenezi.

30 Ubatizo wa Yohane uchokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu? Mundiyankhe.

31 Ndipo anatsutsana mwa iwo okha, nanena, Tikati, Kumwamba; adzanena Iye, Ndipo simunakhulupirire iye bwanji?

32 Koma tikati, Kwa anthu, anaopa anthuwo; pakuti onse anamuyesa Yohanemnenerindithu.

33 Ndipo iwo anamyankha Yesu, ananena nao, Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndichita nao zinthu zimenezi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/11-fb491d5d1e8734a2a6fb421b36b4085d.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 12

Fanizo la osungira munda

1 Ndipo Iye anayamba kulankhula nao m’mafanizo. Munthu analima munda wampesa, nauzunguniza ndi linga, nakumba moponderamo mphesa, namanga nsanja, naukongoletsa kwa olima munda, namuka kwina.

2 Ndipo m’nyengo yake anatuma kapolo kwa olimawo, kuti alandireko kwa olimawo zipatso za m’munda wampesa.

3 Ndipo iwo anamtenga iye, nampanda, namchotsa wopanda kanthu.

4 Ndipo anatumanso kapolo wina kwa iwo; ndipo ameneyu anamlasa mutu, namchitira zomchititsa manyazi.

5 Ndipo anatuma wina; iyeyu anamupha; ndi ena ambiri; ena anawapanda, ndi ena anawapha.

6 Anamtsalira mmodzi, ndiye mwana wake wokondedwa; potsiriza anamtuma iye kwa iwo, nanena, Adzamchitira ulemu mwana wanga.

7 Koma olima ajawo, ananena mwa iwo okha, Ameneyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe iye, ndipo mundawu udzakhala wathu.

8 Ndipo anamtenga, namupha iye, namtaya kunja kwa munda.

9 Pamenepo mwini munda adzachita chiyani? Adzafika, nadzaononga olimawo, nadzapereka mundawo kwa ena.

10 Kodi simunawerenge ngakhale lembo ili,

Mwala umene anaukana omanga nyumba,

womwewu unayesedwa mutu wa pangodya:

11 Ichi chinachokera kwa Ambuye,

ndipo chili chozizwitsa m’maso mwathu?

12 Ndipo anayesa kumgwira Iye; koma anaopa khamu la anthu, pakuti anazindikira kuti Iye anakamba fanizo ili kuwatsutsa iwo; ndipo anamsiya Iye, nachoka.

Za kupereka msonkho

13 Ndipo anatuma kwa Iye ena aAfarisindi a Aherode, kuti akamkole Iye m’kulankhula kwake.

14 Ndipo pamene anafika, ananena naye, Mphunzitsi, tidziwa kuti muli woona, ndipo simusamala munthu; pakuti simuyang’ana nkhope ya anthu, koma muphunzitsa njira ya Mulungu moona: Nkuloleka kodi kupereka msonkho kwaKaisara, kapena iai?

15 Kodi tipereke kapena tisapereke? Koma Iye anadziwa chinyengo chao, nati kwa iwo, Mundiyeseranji? Nditengereni rupiya latheka, kuti ndilione. Ndipo analitenga.

16 Ndipo ananena nao, Chithunzithunzi ichi, ndi chilembo chake zili za yani? Ndipo anati kwa Iye, Za Kaisara,

17 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Perekani zake za Kaisara kwa Kaisara, ndi zake za Mulungu kwa Mulungu. Ndipo anazizwa naye kwambiri.

Asaduki afunsa za kuuka kwa akufa

18 Ndipo anadza kwa IyeAsaduki, amene amanena kuti palibe kuuka kwa akufa; ndipo anamfunsa Iye, nanena,

19 Mphunzitsi, Mose anatilembera, kuti, Akafa mbale wake wa munthu, nasiya mkazi, wosasiya mwana, mbale wake atenge mkazi wake, namuukitsire mbale wakeyo mbeu.

20 Analipo abale asanu ndi awiri; woyamba anakwatira mkazi, nafa, wosasiya mbeu;

21 ndipo wachiwiri anamkwatira, nafa, wosasiya mbeu; ndipo wachitatunso anatero momwemo;

22 ndipo asanu ndi awiriwo analibe kusiya mbeu. Potsiriza pake pa onse mkazinso anafa.

23 Pakuuka adzakhala mkazi wa yani wa iwowa? Pakuti asanu ndi awiriwo adamuyesa mkazi wao.

24 Yesu ananena nao, Simusochera nanga mwa ichi, popeza mulibe kudziwa malembo, kapena mphamvu yake ya Mulungu?

25 Pakuti pamene adzauka kwa akufa, sakwatira, kapena sakwatiwa; koma akhala ngatiangeloa Kumwamba. Koma za akufa, kuti akaukitsidwa;

26 simunawerenga m’buku la Mose kodi, za chitsambacho, kuti Mulungu anati kwa iye, nanena, Ine Ndine Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isaki, ndi Mulungu wa Yakobo?

27 Sali Mulungu wa akufa, koma wa amoyo: musochera inu ndithu.

Lamulo loposa onse

28 Ndipo anadza mmodzi wa alembi, namva iwo alikufunsana pamodzi, ndipo pakudziwa kuti anawayankha bwino, anamfunsa Iye, Lamulo la m’tsogolo la onse ndi liti?

29 Yesu anayankha, kuti, La m’tsogolo ndili, Mvera, Israele; Ambuye Mulungu wathu, Ambuye ndiye mmodzi;

30 ndipo uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mphamvu yako yonse.

31 Lachiwiri ndi ili, Uzikonda mnzako monga udzikonda mwini. Palibe lamulo lina lakuposa awa.

32 Ndipo mlembiyo anati kwa Iye, Chabwino, Mphunzitsi, mwanena zoona kuti ndiye mmodzi; ndipo palibe wina, koma Iye:

33 ndipo, kumkonda Iye ndi mtima wonse, ndi nzeru yonse, ndi mphamvu yonse, ndi kukonda mnzake monga adzikonda mwini, ndiko kuposa nsembe zopsereza zamphumphu zonse, ndi nsembe zophedwa.

34 Ndipo pakuona kuti anayankha ndi nzeru, Yesu anati kwa iye, Suli kutali ndi Ufumu wa Mulungu. Ndipo palibe munthu analimbanso mtima kumfunsa Iye kanthu.

Khristu mwana wa Davide

35 Ndipo Yesu pamene anaphunzitsa mu Kachisi, anayankha, nanena, Bwanji alembi anena kutiKhristundiye mwana wa Davide?

36 Davide mwini yekha anati mwa Mzimu Woyera, Ambuye anati kwa Ambuye wanga, Khala kudzanja langa lamanja, kufikira ndiwaika adani ako popondapo mapazi ako.

37 Davide mwini yekha amtchula Iye Ambuye; ndipo ali mwana wake bwanji? Ndipo anthu a makamuwo anakondwa kumva Iye.

Yesu awachenjeza za Alembi

38 Ndipo m’chiphunzitso chake ananena, Yang’anirani mupewe alembi, akufuna kuyendayenda ovala miinjiro, ndi kulonjeredwa pamisika,

39 ndi kukhala nayo mipando yaulemu m’sunagoge, ndi malo aulemu pamaphwando:

40 amenewo alusira nyumba za akazi amasiye, napemphera monyenga mau ambiri; amenewa adzalandira kulanga koposa.

Mphatso ya mkazi wamasiye

41 Ndipo Iye anakhala pansi pandunji pa mosungiramo ndalama, napenya kuti khamu la anthu alikuponya ndalama mosungiramo; ndipo eni chuma ambiri anaponyamo zambiri.

42 Ndipo anadza mkazi wamasiye waumphawi, ndipo iye anaponyamo tindalama tiwiri tating’ono tokwanira kakobiri kamodzi.

43 Ndipo anaitanaophunziraake, nati kwa iwo, Ndithu ndinena ndi inu, Mkazi wamasiye amene waumphawi anaponya zambiri koposa onse akuponya mosungiramo:

44 pakuti anaponyamo onse mwa zochuluka zao; koma iye anaponya mwa kusowa kwake zonse anali nazo, inde moyo wake wonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/12-49808ba024d1d004e935a63d8de06d00.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 13

Yesu aneneratu za masautso alinkudza

1 Ndipo pamene analikutuluka Iye mu Kachisi, mmodzi waophunziraake ananena kwa Iye, Mphunzitsi, onani, miyala yotere ndi nyumba yotere.

2 Ndipo Yesu anati kwa iye, Kodi waona nyumba izi zazikulu? Sudzasiyidwa pano mwala umodzi pamwamba pa unzake, umene sudzagwetsedwa.

3 Ndipo pamene anakhala Iye paphiri la Azitona, popenyana ndi Kachisi, anamfunsa Iye m’tseri Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, ndi Andrea, kuti,

4 Tiuzeni, zinthu izi zidzachitika liti? Ndi chotani chizindikiro chake chakuti zili pafupi pa kumalizidwa zinthu izi zonse?

5 Ndipo Yesu anayamba kunena nao, Yang’anirani kuti munthu asakusocheretseni.

6 Ambiri adzafika m’dzina langa, nadzanena, Ine ndine Iye; nadzasocheretsa ambiri.

7 Ndipo m’mene mudzamva za nkhondo ndi mbiri zake za nkhondo, musamadera nkhawa: ziyenera kuchitika izi; koma sichinafike chimaliziro.

8 Pakuti mtundu wa anthu udzayambana ndi mtundu wina, ndipo ufumu ndi ufumu unzake: padzakhala zivomezi m’malo m’malo; padzakhala njala; izi ndi zoyambira za zowawa.

9 Koma inu mudziyang’anire inu nokha; pakuti adzakuperekani inu kubwalo la akulu a milandu; ndipo adzakukwapulani m’masunagoge; ndipo pamaso pa akazembe ndi mafumu mudzaimirira chifukwa cha Ine, kukhale umboni kwa iwo.

10 Ndipo Uthenga Wabwino uyenera uyambe kulalikidwa kwa anthu a mitundu yonse.

11 Ndipo pamene adzapita nanu kumlandu, nadzakuperekani, musade nkhawa usanayambe mlandu ndi chimene mudzalankhula; koma chimene chidzapatsidwa kwa inu m’mphindi yomweyo, muchilankhule; pakuti olankhula si ndinu, koma Mzimu Woyera.

12 Ndipo mbale adzapereka mbale wake kuti amuphe, ndi atate mwana wake; ndi ana adzayambana ndi akuwabala, nadzawaphetsa.

13 Ndipo adzada inu anthu onse chifukwa cha dzina langa: koma iye wakupirira kufikira chimaliziro, yemweyo adzapulumutsidwa.

Yesu aneneratu za chisautso chachikulu

14 Ndipo pamene mukaona chonyansa cha kupululutsa chilikuima pomwe sichiyenera (wakuwerenga azindikire), pamenepo a mu Yudeya athawire kumapiri:

15 ndi iye amene ali pamwamba pa tsindwi asatsike, kapena asalowe kukatulutsa kanthu m’nyumba mwake;

16 ndi iye amene ali kumunda asabwere kudzatenga malaya ake.

17 Koma tsoka iwo akukhala ndi pakati, ndi akuyamwitsa ana masiku awo!

18 Ndipo pempherani kuti kusakhale m’nyengo yachisanu.

19 Pakuti masiku aja padzakhala chisautso, chonga sichinakhala chinzake kuyambira chiyambi cha chilengedwe chimene Mulungu anachilenga ndi kufikira tsopano, ndipo sichidzakhalanso, nthawi zonse.

20 Ndipo Ambuye akadapanda kufupikitsa masikuwo, sakadapulumuka munthu mmodzi yense; koma chifukwa cha osankhidwa amene anawasankha, anafupikitsa masikuwo.

21 Ndipo pamenepo wina akati kwa inu, OnaniKhristuali pano; kapena, Onani, uko; musavomereze;

22 pakuti adzauka Akhristu onyenga ndi aneneri onyenga, ndipo adzachita zizindikiro ndi zozizwitsa, kuti akasocheretse, ngati nkutheka, osankhidwa omwe.

23 Koma yang’anirani; onani ndakuuziranitu zinthu zonse, zisanafike.

Yesu aneneratu kuti adzabwera

24 Koma m’masikuwo, chitatha chisautso chimenecho, dzuwa lidzadetsedwa, ndi mwezi sudzapatsa kuunika kwake,

25 ndi nyenyezi zidzagwa kuchokera m’mwamba ndi mphamvu zili m’mwamba zidzagwedezeka.

26 Ndipo pamenepo adzaonaMwana wa Munthualinkudza m’mitambo ndi mphamvu yaikulu, ndi ulemerero.

27 Ndipo pamenepo adzatumaangelo, nadzasonkhanitsa osankhidwa ake ochokera kumphepo zinai, kuyambira ku malekezero ake a dziko lapansi, ndi kufikira ku malekezero a thambo.

28 Ndipo phunzirani ndi mkuyufanizolake; pamene pafika kuti nthambi yake ikhala yanthete, ndipo anaphuka masamba ake, muzindikira kuti layandikira dzinja;

29 chomwecho inunso, pamene muona zinthu izi zilikuchitika, zindikirani kuti ali pafupi pakhomo.

30 Indetu ndinena ndi inu, Mbadwo uno sudzapita kufikira zinthu izi zonse zitachitika.

31 Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.

32 Koma za tsiku ilo, kapena nthawi yake sadziwa munthu, angakhale angelo mu Mwamba, angakhale Mwana, koma Atate ndiye.

Za kulindirira

33 Yang’anirani, dikirani, pempherani: pakuti simudziwa nthawi yake.

34 Monga ngati munthu wa paulendo, adachoka kunyumba kwake, nawapatsa akapolo ake ulamuliro, kwa munthu aliyense ntchito yake, nalamula wapakhomo adikire.

35 Chifukwa chake dikirani; pakuti simudziwa inu nthawi yake yakubwera mwini nyumba, kapena madzulo, kapena pakati pausiku, kapena pakulira tambala, kapena mamawa;

36 kuti angabwere balamanthu nakakupezani muli m’tulo.

37 Ndipo chimene ndinena ndi inu ndinena kwa onse, Dikirani.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/13-6d200414ac6ff9cc911b0268c801a7dc.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 14

Ansembe aakulu achita chiwembu pa Yesu

1 Ndipo popita masiku awiri kuli phwando laPaskandi Mkate wopanda chotupitsa; ndipo ansembe aakulu ndi alembi anafunafuna momchitira chiwembu, ndi kumupha:

2 pakuti anati, Pachikondwerero ai, kuti pangakhale phokoso la anthu.

Phwando la ku Betaniya

3 Ndipo pakukhala Iye ku Betaniya m’nyumba ya Simoni wakhate, m’mene anaseama kudya, anadzapo mkazi ali nayo nsupa ya alabastero ya mafuta onunkhira bwino anaridoweniweni a mtengo wapatali; naswa nsupayo, nawatsanulira pamutu pake.

4 Koma anakhalako ena anavutika mtima mwa iwo okha, ndi kuti, Mafutawo atayidwa chifukwa ninji?

5 Pakuti mafuta amene akadagula marupiya atheka mazana atatu ndi mphamvu zake, ndi kupatsa aumphawi. Ndipo anadandaulira mkaziyo.

6 Koma Yesu anati, Mlekeni, mumvutiranji? Wandichitira Ine ntchito yabwino.

7 Pakuti muli nao aumphawi pamodzi ndi inu masiku onse, ndipo paliponse pamene mukafuna mukhoza kuwachitira zabwino; koma Ine simuli nane masiku onse.

8 Iye wachita chimene wakhoza; anandidzozeratu thupi langa ku kuikidwa m’manda.

9 Ndipo ndithu ndinena ndi inu, Ponse pamene padzalalikidwa Uthenga Wabwino kudziko lonse lapansi, ichinso chimene anachita mkazi uyu chidzanenedwa, chikhale chomkumbukira nacho.

Yudasi apangana ndi ansembe aakulu

10 Ndipo Yudasi Iskariote, ndiye mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anachoka napita kwa ansembe aakulu, kuti akampereke Iye kwa iwo.

11 Ndipo pamene iwo anamva, anasekera, nalonjezana naye kuti adzampatsa ndalama. Ndipo iye anafunafuna pompereka Iye bwino.

Paska wotsiriza

12 Ndipo tsiku loyamba la mikate yopanda chotupitsa, pamene amapha Paska,ophunziraananena naye, Mufuna tinke kuti, tikakonze mkadyereko Paska?

13 Ndipo anatuma awiri a ophunzira ake, nanena nao, Lowani m’mzinda, ndipo adzakomana nanu munthu wakusenza mtsuko wa madzi; mumtsate iye;

14 ndipo kumene akalowako iye, munene naye mwini nyumba, Mphunzitsi anena, Chilikuti chipinda cha alendo changa, m’menemo ndikadye Paska ndi ophunzira anga?

15 Ndipo iye yekha adzakusonyezani chipinda chapamwamba chachikulu choyalamo ndi chokonzedwa; ndipo m’menemo mutikonzere.

16 Ndipo ophunzira anatuluka, nafika m’mzinda, napeza monga anati kwa iwo; ndipo anakonza Paska.

17 Ndipo pofika madzulo anadza Iye pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.

18 Ndipo pamene anaseama iwo kudya, Yesu anati, Ndithu ndinena ndi inu, Mmodzi wa inu adzandipereka Ine, ndiye wakudya ndi Ine pamodzi.

19 Anayamba iwo kukhala ndi chisoni, ndi kunena naye mmodzimmodzi, kuti, Ndine kodi?

20 Ndipo anati kwa iwo, Mmodzi wa khumi ndi awiriwo, ndiye wakusunsa pamodzi ndi Ine m’mbale.

21 Pakuti Mwana wa Munthu amukadi, monga kwalembedwa za Iye; koma tsoka munthuyo amene apereka Mwana wa Munthu! Kukadakhala bwino kwa munthu ameneyo ngati sakadabadwa iye.

Mgonero wa Ambuye

22 Ndipo pamene iwo analikudya, Iye anatenga mkate, ndipo pamene anadalitsa, ananyema, napereka kwa iwo, kuti, Tengani; thupi langa ndi ili.

23 Ndipo anatenga chikho, ndipo pamene adayamika, anapereka kwa iwo; ndipo iwo onse anamweramo.

24 Ndipo Iye anati kwa iwo, Ichi ndi mwazi wanga wachipangano, wothiridwa chifukwa cha anthu ambiri.

25 Ndithu ndinena nanu, Sindidzamwanso chipatso cha mpesa, kufikira tsiku lijalo, limene ndidzamwa icho chatsopano mu Ufumu wa Mulungu.

26 Ndipo ataimba nyimbo, anatuluka, namuka kuphiri la Azitona.

Yesu achenjeza Petro

27 Ndipo Yesu ananena nao, Mudzakhumudwa nonsenu; pakuti kwalembedwa,

Ndidzakantha mbusa, ndi nkhosa zidzamwazika.

28 Komatu nditadzauka ndidzatsogolera inu ku Galileya.

29 Koma Petro ananena naye, Angakhale adzakhumudwa onse, komatu ine iai.

30 Ndipo Yesu ananena naye, Ndithu ndinena ndi iwe, kuti lero, usiku uno, tambala asanalire kawiri, udzandikana Ine katatu.

31 Koma iye analimbitsa mau chilimbitsire, kuti, Ngakhale ndidzafa nanu, sindidzakana Inu. Ndipo onsewo anatero.

Getsemani

32 Ndipo iwo anadza kumalo dzina lake Getsemani; ndipo ananena kwa ophunzira ake, Bakhalani pano, kufikira ndikapemphera.

33 Ndipo anatenga pamodzi ndi Iye Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, nayamba kudabwa kwambiri, ndi kusauka mtima ndithu.

34 Ndipo ananena nao, Moyo wanga uli wa chisoni chambiri, kufikira imfa. Bakhalani pano, nimundikire.

35 Ndipo Iye anapita m’tsogolo pang’ono, nagwa pansi, napemphera kuti ngati nkutheka nthawi imene impitirire.

36 Ndipo ananena,Abba, Atate, zinthu zonse zitheka ndi Inu; mundichotsere chikho ichi; komatu si chimene ndifuna Ine, koma chimene mufuna Inu.

37 Ndipo anadza nawapeza iwo ali m’tulo, nanena ndi Petro, Simoni, ugona kodi? Unalibe mphamvu yakudikira ora limodzi kodi?

38 Dikirani, pempherani, kuti mungalowe m’kuyesedwa; mzimutu uli wakufuna, koma thupi lili lolefuka.

39 Ndipo anachokanso, napemphera, nanena mau omwewo.

40 Ndipo anadzanso nawapeza ali m’tulo, pakuti maso ao analemeradi; ndipo sanadziwe chomyankha Iye.

41 Ndipo anadza kachitatu, nanena nao, Gonani tsopano, nimupumule; chakwanira; yafika nthawi; onani Mwana wa Munthu aperekedwa m’manja a anthu ochimwa.

42 Ukani, tizimuka; onani wakundiperekayo ali pafupi.

Amgwira Yesu

43 Ndipo pomwepo, Iye ali chilankhulire, anadza Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, ndipo pamodzi naye khamu la anthu, ali nao malupanga ndi mikunkhu, ochokera kwa ansembe aakulu ndi alembi ndi akulu.

44 Ndipo wakumpereka Iye anawapatsa chizindikiro, nanena, Iye amene ndidzampsompsona, ndiyetu; mgwireni munke naye chisungire.

45 Ndipo atafika, pomwepo anadza kwa Iye, nanena,Rabi; nampsompsonetsa.

46 Ndipo anamthira manja, namgwira.

47 Koma mmodzi wina wa iwo akuimirirapo, anasolola lupanga lake, nakantha kapolo wake wa mkulu wa ansembe, namdula khutu lake.

48 Ndipo Yesu anayankha nati kwa iwo, Kodi mwatuluka ndi malupanga ndi mikunkhu kundigwira Ine monga wachifwamba?

49 Masiku onse ndinali nanu mu Kachisi ndilikuphunzitsa, ndipo simunandigwire Ine; koma ichi chachitika kuti malembo akwaniritsidwe.

50 Ndipo iwo onse anamsiya Iye, nathawa.

51 Ndipo mnyamata wina anamtsata Iye, atafundira pathupi nsalu yabafuta yokha; ndipo anamgwira;

52 koma iye anasiya nsaluyo, nathawa wamaliseche.

Yesu aweruzidwa ndi akulu a Ayuda

53 Ndipo ananka naye Yesu kwa mkulu wa ansembe; ndipo anasonkhana kwa iye ansembe aakulu onse ndi akulu a anthu, ndi alembi.

54 Ndipo Petro adamtsata Iye kutali, kufikira kulowa m’bwalo la mkulu wa ansembe; ndipo anali kukhala pansi pamodzi ndi anyamata, ndi kuotha moto.

55 Ndipo ansembe aakulu ndi akulu a milandu onse anafunafuna umboni wakutsutsa nao Yesu kuti amuphe Iye; koma sanaupeze.

56 Pakuti ambiri anamchitira umboni wonama, ndipo umboni wao sunalingane.

57 Ndipo ananyamukapo ena, namchitira umboni wakunama, nanena kuti,

58 Ife tinamva Iye alikunena, kuti, Ine ndidzaononga Kachisi uyu wopangidwa ndi manja, ndi masiku atatu ndidzamanga wina wosapangidwa ndi manja.

59 Ndipo ngakhale momwemo umboni wao sunalingane.

60 Ndipo mkulu wa ansembe ananyamuka pakati, namfunsa Yesu, nanena, Suyankha kanthu kodi? Nchiyani ichi chimene awa alikuchitira mboni?

61 Koma anakhala chete, osayankha kanthu. Mkulu wa ansembe anamfunsanso, nanena naye, Kodi Iwe ndiwe Khristu, Mwana wake wa Wolemekezeka?

62 Ndipo Yesu anati, Ndine amene; ndipo mudzaona Mwana wa Munthu alikukhala kudzanja lamanja la mphamvu, ndi kudza ndi mitambo ya kumwamba.

63 Ndipo mkulu wa ansembe anang’amba malaya ake, nanena, Tifuniranjinso mboni zina?

64 Mwamva mwano wake; muyesa bwanji? Ndipo onse anamtsutsa Iye kuti ayenera kufa.

65 Ndipo ena anayamba kumthira malovu Iye, ndi kuphimba nkhope yake, ndi kumbwanyula, ndi kunena naye, Lota; ndipo anyamatawo anampanda Iye khofu.

Petro akana kuti sadziwa Yesu

66 Ndipo pamene Petro anali pansi m’bwalo, anadzapo mmodzi wa adzakazi a mkulu wa ansembe;

67 ndipo anaona Petro alikuotha moto, namyang’ana iye, nanena, Iwenso unali naye Mnazarene, Yesu.

68 Koma anakana, nanena, Sindidziwa kapena kumvetsa chimene uchinena iwe; ndipo anatuluka kunka kuchipata; ndipo tambala analira.

69 Ndipo anamuona mdzakaziyo, nayambanso kunena ndi iwo akuimirirapo, Uyu ngwa awo.

70 Koma anakananso. Ndipo patapita kamphindi, akuimirirapo ananenanso ndi Petro, Zedi uli wa awo; pakutinso uli Mgalileya.

71 Koma iye anayamba kutemberera, ndi kulumbira, Sindimdziwa munthuyu mulikunena.

72 Ndipo pomwepo tambala analira kachiwiri. Ndipo Petro anakumbukira umo Yesu anati kwa iye, kuti, Tambala asanalire kawiri udzandikana katatu. Ndipo pakuganizira ichi analira misozi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/14-573e5591b496bf8172db623563b120c7.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 15

Yesu aweruzidwa ndi Pilato

1 Ndipo pomwepo mamawa anakhala upo ansembe aakulu, ndi akulu a anthu, ndi alembi, ndi akulu a milandu onse, namanga Yesu, namtenga, nampereka kwa Pilato.

2 Ndipo Pilato anamfunsa Iye, Kodi ndiwe mfumu ya Ayuda? Ndipo anayankha, nanena naye, Mwatero.

3 Ndipo ansembe aakulu anamnenera Iye zinthu zambiri.

4 Ndipo Pilato anamfunsanso, nanena, Suyankha kanthu kodi? Taona, akunenera Iwe zinthu zambiri zotere.

5 Koma Yesu sanayankhenso kanthu; kotero kuti Pilato anazizwa.

6 Ndipo ankawamasulira pachikondwerero wandende mmodzi, amene iwo anampempha.

7 Ndipo analipo wina dzina lake Barabasi, womangidwa pamodzi ndi opanduka, amene anapha munthu mumpanduko.

8 Ndipo khamu la anthu anabwera nayamba kupempha kuti achite monga anali kuwachitira nthawi zonse.

9 Ndipo Pilato anawayankha, nanena nao, Kodi mufuna kuti ndikumasulireni mfumu ya Ayuda?

10 Pakuti anazindikira kuti ansembe aakulu anampereka Iye mwanjiru.

11 Koma ansembe aakulu anasonkhezera khamulo, kuti makamaka awamasulire Barabasi.

12 Ndipo Pilato anawayankhanso, nati kwa iwo, Pamenepo ndidzachita chiyani ndi Iye amene mumtchula mfumu ya Ayuda?

13 Ndipo anafuulanso, Mpachikeni pamtanda.

14 Ndipo Pilato ananena nao, Pakuti Iye anachita choipa chotani? Koma iwo anafuulitsatu, Mpachikeni Iye.

15 Ndipo Pilato pofuna kuwakhazika mtima anthuwo, anawamasulira Barabasi, napereka Yesu, atamkwapula, akampachike pamtanda.

16 Ndipo asilikali anachoka naye nalowa m’bwalo, ndilo Pretorio; nasonkhanitsa gulu lao lonse.

17 Ndipo anamveka Iye chibakuwa, naluka korona waminga, namveka pa Iye;

18 Ndipo anayamba kumlankhula Iye, kuti, Tikuoneni, mfumu ya Ayuda!

19 Ndipo anampanda Iye pamutu pake ndi bango, namthira malovu, nampindira maondo, namlambira.

20 Ndipo atatha kumnyoza anamvula chibakuwacho namveka Iye zovala zake. Ndipo anatuluka naye kuti akampachike Iye pamtanda.

Ampachika Yesu pamtanda

21 Ndipo anakakamiza wina wopitirirapo, Simoni wa ku Kirene, alikuchokera kuminda, atate wao wa Aleksandro ndi Rufu, kuti anyamule mtanda wake.

22 Ndipo anamtenga kunka naye kumalo Gologota, ndiwo, osandulika, Malo a Bade.

23 Ndipo anampatsa vinyo wosakaniza ndimure; koma Iye sanamlandire.

24 Ndipo anampachika Iye, nagawana zovala zake mwa iwo okha, ndi kuchita maere pa izo, kuti adziwe yense adzatenga chiyani.

25 Ndipo panali ora lachitatu, ndipo anampachika Iye.

26 Ndipo lembo la mlandu wake linalembedwa pamwamba, MFUMU YA AYUDA.

27 Ndipo anapachika pamodzi ndi Iye achifwamba awiri; mmodzi kudzanja lake lamanja ndi wina kulamanzere.

29 Ndipo iwo akupitirirapo anamchitira mwano, napukusa mitu yao, nanena, Ha! Iwe wakupasula Kachisi, ndi kummanga masiku atatu,

30 udzipulumutse mwini, nutsike pamtanda.

31 Moteronso ansembe aakulu anamtonza mwa iwo okha pamodzi ndi alembi, nanena, Anapulumutsa ena; sangathe kudzipulumutsa yekha.

32 Atsike tsopano pamtanda,Khristumfumu ya Israele, kuti tione, ndi kukhulupirira. Ndipo iwo akupachikidwa naye anamlalatira.

Yesu afa pamtanda

33 Ndipo pofika ora lachisanu ndi chimodzi, panali mdima padziko lonse, kufikira ora lachisanu ndi chinai.

34 Ndipo pa ora lachisanu ndi chinai Yesu anafuula ndi mau okweza,Eloi, Eloi, lama sabakitani?ndiko kusandulika,

Mulungu wanga, Mulungu wanga mwandisiyiranji Ine?

35 Ndipo ena akuimirirapo, pakumva, ananena, Taonani, aitana Eliya.

36 Ndipo anathamanga wina, nadzaza chinkhupule ndi vinyo wosasa, nachiika pabango, namwetsa Iye, nanena, Lekani; tione ngati Eliya adza kudzamtsitsa.

37 Ndipo Yesu anatulutsa mau okweza, napereka mzimu wake.

38 Ndipo chinsalu chotchinga cha mu Kachisi chinang’ambika pakati, kuyambira kumwamba kufikira pansi.

39 Ndipo pamenekenturiyo, woimirirapo popenyana ndi Iye, anaona kuti anapereka mzimu kotero, anati, Zoonadi, munthu uyu anali Mwana wa Mulungu.

40 Ndipo analinso kumeneko akazi akuyang’anira kutali; mwa iwo anali Maria wa Magadala, ndi Maria amake wa Yakobo wamng’ono ndi wa Yosefe, ndi Salome;

41 amene anamtsata Iye, pamene anali mu Galileya, namtumikira; ndi akazi ena ambiri, amene anakwera kudza ndi Iye kuYerusalemu.

Yesu aikidwa m’manda

42 Ndipo atafika tsono madzulo, popeza mpa tsiku lokonzekera, ndilo la pambuyo paSabata,

43 anadzapo Yosefe wa ku Arimatea, mkulu wa milandu womveka, amene yekha analikuyembekezera Ufumu wa Mulungu; nalimba mtima nalowa kwa Pilato, napempha mtembo wake wa Yesu.

44 Ndipo Pilato anazizwa ngati adamwaliradi; naitana kenturiyo, namfunsa ngati adamwalira kale.

45 Ndipo pamene anachidziwa ndi kenturiyo, anamninkha Yosefe mtembowo.

46 Ndipo anagula bafuta, namtsitsa Iye, namkulunga m’bafutamo, namuika m’manda osemedwa m’thanthwe; nakunkhunizira mwala pakhomo la manda.

47 Ndipo Maria wa Magadala ndi Maria amake wa Yosefe anapenya pomwe anaikidwapo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/15-7d67cb9447ef586d9640862f5b6a4c78.mp3?version_id=1068—

Categories
MARKO

MARKO 16

Yesu auka kwa akufa

1 Ndipo litapitaSabata, Maria wa Magadala, ndi Maria amake wa Yakobo, ndi Salome, anagula zonunkhira, kuti akadze kumdzoza Iye.

2 Ndipo anadza kumanda mamawa tsiku loyamba la Sabata, litatuluka dzuwa.

3 Ndipo analikunena mwa okha, Adzatikunkhunizira ndani mwalawo, pakhomo la manda?

4 Ndipo pamene anakweza maso anaona kuti mwala wakunkhunizidwa, pakuti unali waukulu ndithu.

5 Ndipo pamene analowa m’manda, anaona mnyamata alikukhala kumbali ya kudzanja lamanja, wovala mwinjiro woyera; ndipo iwo anadabwa.

6 Ndipo iye ananena nao, Musadabwe: mulikufuna Yesu Mnazarene amene anapachikidwa; anauka; sali pano; taonani, mbuto m’mene anaikamo Iye!

7 Koma mukani, uzaniophunziraake, ndi Petro, kuti akutsogolerani inu ku Galileya; kumeneko mudzamuona Iye, monga ananena ndi inu.

8 Ndipo anatuluka iwo, nathawa kumanda; pakuti kunthunthumira ndi kudabwa kwakukulu kudawagwira; ndipo sanauze kanthu kwa munthu aliyense; pakuti anachita mantha.

Yesu aonekera kwa ophunzira ake

9 Ndipo pamene Iye adauka mamawa tsiku loyamba la sabata, anayamba kuonekera kwa Maria wa Magadala, amene Iye adamtulutsira ziwanda zisanu ndi ziwiri.

10 Iyeyu anapita kuwauza iwo amene ankakhala naye, ali ndi chisoni ndi kulira misozi.

11 Ndipo iwowo, pamene anamva kuti ali moyo, ndi kuti adapenyeka kwa iye, sanamvere.

12 Ndipo zitatha izi, anaonekanso Iye m’maonekedwe ena kwa awiri a iwo alikuyenda kupita kumidzi.

13 Ndipo iwowa anachoka nawauza otsala; koma iwo omwe sanawavomereze.

14 Ndipo chitatha icho anaonekera kwa khumi ndi mmodzi iwo okha, alikuseama pachakudya; ndipo anawadzudzula chifukwa cha kusavomereza kwao ndi kuuma mtima, popeza sanavomereze iwo amene adamuona, atauka Iye.

15 Ndipo ananena nao, Mukani kudziko lonse lapansi, lalikirani Uthenga Wabwino kwa olengedwa onse.

16 Amene akhulupirira nabatizidwa, adzapulumutsidwa; koma amene sakhulupirira adzalangidwa.

17 Ndipo zizindikiro izi zidzawatsata iwo akukhulupirira: m’dzina langa adzatulutsa ziwanda; adzalankhula ndi malankhulidwe atsopano;

18 adzatola njoka, ndipo ngakhale akamwa kanthu kakufa nako, sikadzawapweteka; adzaika manja ao pa odwala, ndipo adzachira.

19 Pamenepo Ambuye Yesu, atatha kulankhula nao, analandiridwa Kumwamba, nakhala padzanja lamanja la Mulungu.

20 Ndipo iwowa anatuluka, nalalikira ponseponse, ndipo Ambuye anachita nao pamodzi, natsimikiza mau ndi zizindikiro zakutsatapo.Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/MRK/16-e61ac6f0ef6fafd88a5facb0f37dbc0b.mp3?version_id=1068—