Kenturiyo Kornelio
1 Ndipo kunali munthu ku Kesareya, dzina lake Kornelio,kenturiyowa gulu lotchedwa la Italiya,
2 ndiye munthu wopembedza, ndi wakuopa Mulungu ndi banja lake lonse, amene anapatsa anthu zachifundo zambiri, napemphera Mulungu kosaleka.
3 Iye anapenya m’masomphenya poyera,mngelowa Mulungu alinkudza kwa iye, ngati ora lachisanu ndi chinai la usana, nanena naye, Kornelio.
4 Ndipo pompenyetsetsa iye ndi kuopa, anati, Nchiyani, Mbuye? Ndipo anati kwa iye, Mapemphero ako ndi zachifundo zako zinakwera zikhala chikumbutso pamaso pa Mulungu.
5 Ndipo tsopano tumiza amuna ku Yopa, aitane munthu Simoni, wotchedwanso Petro;
6 acherezedwa iye ndi wina Simoni wofufuta zikopa, nyumba yake ili m’mbali mwa nyanja.
7 Ndipo m’mene atachoka mngelo amene adalankhula naye, anaitana anyamata ake awiri, ndi msilikali wopembedza, wa iwo amene amtumikira kosaleka;
8 ndipo m’mene adawafotokozera zonse, anawatuma ku Yopa.
9 Koma m’mawa mwake, pokhala paulendo pao iwowa, m’mene anayandikira mzinda, Petro anakwera patsindwi kukapemphera, ngati pa ora lachisanu ndi chimodzi; ndipo anagwidwa njala, nafuna kudya;
10 koma m’mene analikumkonzera chakudya kudamgwera ngati kukomoka;
11 ndipo anaona pathambo padatseguka, ndi chotengera chilinkutsika, chonga ngati chinsalu chachikulu, chogwiridwa pangodya zake zinai, ndi kutsikira padziko pansi;
12 m’menemo munali nyama za miyendo inai za mitundu yonse, ndi zokwawa za padziko ndi mbalame za m’mlengalenga.
13 Ndipo anamdzera mau, Tauka, Petro; ipha, mudye.
14 Koma Petro anati, Iaitu, Mbuye; pakuti sindinadye ine ndi kale lonse kanthu wamba ndi konyansa.
15 Ndipo mau anamdzeranso nthawi yachiwiri, Chimene Mulungu anayeretsa, usachiyesa chinthu wamba.
16 Ndipo chinachitika katatu ichi; ndipo pomwepo chotengeracho chinatengedwa kunka kumwamba.
17 Ndipo pokayikakayika Petro mwa yekha ndi kuti masomphenya adawaona akuti chiyani, taonani, amuna aja otumidwa ndi Kornelio, atafunsira nyumba ya Simoni, anaima pachipata,
18 ndipo anaitana nafunsa ngati Simoni, wotchedwanso Petro, acherezedwako.
19 Ndipo m’mene Petro analingirira za masomphenya, Mzimu anenana naye, Taona, amuna atatu akufuna iwe.
20 Komatu tauka, nutsike, ndipo upite nao, wosakayikakayika; pakuti ndawatuma ndine.
21 Ndipo Petro anatsikira kwa anthuwo, nati, Taonani, ine ndine amene mumfuna; chifukwa chake mwadzera nchiyani?
22 Ndipo anati, Kornelio kenturiyoyo, munthu wolungama ndi wakuopa Mulungu, amene mtundu wonse wa Ayuda umchitira umboni, anachenjezedwa ndi mngelo woyera kuti atumize nakuitaneni mumuke kunyumba yake, ndi kumvetsa mau anu.
23 Pamenepo anawalowetsa nawachereza.
Ndipo m’mawa mwake ananyamuka natuluka nao, ndi ena a abale a ku Yopa anamperekeza iye.
24 Ndipo m’mawa mwake analowa mu Kesareya. Koma Kornelio analikudikira iwo, atasonkhanitsa abale ake ndi mabwenzi ake enieni.
25 Ndipo panali pakulowa Petro, Kornelio anakomana naye, nagwa pa mapazi ake, namlambira.
26 Koma Petro anamuutsa iye, nanena, Nyamuka; inenso ndine munthu.
27 Ndipo pakukamba naye, analowa, napeza ambiri atasonkhana;
28 ndipo anati kwa iwo, Mudziwa inu nokha kuti sikuloledwa kwa munthu Myuda adziphatike kapena kudza kwa munthu wa mtundu wina; koma Mulungu anandionetsera ine ndisanenere aliyense ali munthu wamba kapena wonyansa;
29 chifukwa chakenso ndinadza wosakana, m’mene munatuma kundiitana. Pamenepo ndifunsa, mwandiitaniranji?
30 Ndipo Kornelio anati, Atapita masiku anai, kufikira monga ora ili, ndinalikupemphera m’nyumba yanga pa ora lachisanu ndi chinai; ndipo taonani, padaimirira pamaso panga munthu wovala chovala chonyezimira,
31 nati Kornelio, lamveka pemphero lako, ndi zopereka zachifundo zako zakumbukika pamaso pa Mulungu.
32 Chifukwa chake tumiza anthu ku Yopa, akaitane Simoni amene anenedwanso Petro; amene acherezedwa m’nyumba ya Simoni wofufuta zikopa, m’mbali mwa nyanja.
33 Pamenepo ndinatumiza kwa inu osachedwa; ndipo mwachita bwino mwadza kuno. Chifukwa chake taonani tilitonse pano pamaso pa Mulungu, kumva zonse Ambuye anakulamulirani.
34 Ndipo Petro anatsegula pakamwa pake, nati, Zoona ndizindikira kuti Mulungu alibe tsankho;
35 koma m’mitundu yonse, wakumuopa Iye ndi wakuchita chilungamo alandiridwa naye.
36 Mau amene anatumiza kwa ana a Israele, akulalikira Uthenga Wabwino wa mtendere mwa YesuKhristu(ndiye Ambuye wa onse)
37 mauwo muwadziwa inu, adadzawo ku Yudeya lonse, akuyamba ku Galileya, ndi ubatizo umene Yohane anaulalikira;
38 za Yesu wa ku Nazarete, kuti Mulungu anamdzoza Iye ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu; amene anapitapita nachita zabwino, nachiritsa onse osautsidwa ndi mdierekezi, pakuti Mulungu anali pamodzi ndi Iye.
39 Ndipo ife ndife mboni za zonse adazichita m’dziko la Ayuda ndi muYerusalemu; amenenso anamupha, nampachika pamtengo.
40 Ameneyo, Mulungu anamuukitsa tsiku lachitatu, nalola kuti aonetsedwe,
41 si kwa anthu onse ai, koma kwa mboni zosankhidwiratu ndi Mulungu, ndiwo ife amene tinadya ndi kumwa naye pamodzi, atauka iye kwa akufa.
42 Ndipo anatilamulira ife tilalikire kwa anthu, ndipo tichite umboni kuti Uyu ndiye amene aikidwa ndi Mulungu akhale woweruza amoyo ndi akufa.
43 Ameneyu aneneri onse amchitira umboni, kuti onse akumkhulupirira Iye adzalandira chikhululukiro cha machimo ao, mwa dzina lake.
44 Petro ali chilankhulire, Mzimu Woyera anagwa pa onse akumva mauwo.
45 Ndipo anadabwa okhulupirirawo akumdulidweonse amene anadza ndi Petro, chifukwa pa amitundunso panathiridwa mphatso ya Mzimu Woyera.
46 Pakuti anawamva iwo alikulankhula ndi malilime, ndi kumkuza Mulungu. Pamenepo Petro anayankha,
47 Kodi pali munthu akhoza kuletsa madzi, kuti asabatizidwe awa, amene alandira Mzimu Woyera ngatinso ife?
48 Ndipo analamulira iwo abatizidwe m’dzina la Yesu Khristu. Pamenepo anampempha iye atsotse masiku.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ACT/10-cff5f78829404878e1d33b680f02ccc5.mp3?version_id=1068—