Categories
HOSEYA

HOSEYA 10

1 Israele ndi mpesa wotambalala, wodzibalira wokha zipatso; monga umo zinachulukira zipatso zake, momwemo anachulukitsa maguwa a nsembe ake; monga mwa kukoma kwake kwa dziko lake anapanga zoimiritsa zokoma.

2 Mtima wao wagawikana, tsopano adzapezeka opalamula, adzapasula maguwa ao a nsembe, nadzaononga zoimiritsa zao.

3 Pakuti tsopano adzati, Tilibe mfumu, popeza sitiopa Yehova; ndi mfumu idzatichitira chiyani?

4 Anena mau akulumbira monama, pakuchita mapangano momwemo; chiweruzo chiphuka ngati zitsamba zowawa m’michera ya munda.

5 Okhala mu Samariya adzaopera chifanizo cha anaang’ombe a ku Betaveni; pakuti anthu ake adzamva nacho chisoni, ndi ansembe ake amene anakondwera nacho, chifukwa cha ulemerero wake, popeza unachichokera.

6 Adzachitengeranso ku Asiriya chikhale mphatso ya kwa mfumu Yarebu; Efuremu adzatenga manyazi, ndi Israele adzachita manyazi ndi uphungu wake.

7 Ndipo Samariya, mfumu yake yamwelera ngati thovu pamadzi.

8 Ndipo misanje ya Aveni, ndiyo tchimo la Israele, idzaonongeka; minga ndi mitungwi idzamera pa maguwa ao a nsembe; ndipo adzati kwa mapiri, Tiphimbeni; ndi kwa zitunda, Tigwereni.

9 Israele, wachimwa kuyambira masiku a Gibea; pomwepo anaimabe; nkhondo ya pa ana a chosalungama siinawapeze ku Gibea.

10 Pamene ndifuna ndidzawalanga, ndi mitundu ya anthu idzawasonkhanira pomangidwa iwo pa zolakwa zao ziwiri.

11 Ndipo Efuremu ndiye ng’ombe yaikazi yaing’ono, yozereweredwa, yokonda kupuntha tirigu; koma ndapita pa khosi lake lokoma; ndidzamsenzetsa Efuremu goli; Yuda adzalima, Yakobo adzaphwanya chibuluma chake.

12 Mudzibzalire m’chilungamo mukolole monga mwa chifundo; limani masala anu, pakuti yafika nthawi ya kufuna Yehova, mpaka afika Iye, navumbitsira inu chilungamo.

13 Mwalima choipa, mwakolola chosalungama, mwadya zipatso za mabodza; pakuti watama njira yako ndi kuchuluka kwa anthu ako amphamvu.

14 Momwemo phokoso lidzaukira anthu ako, ndi malinga ako onse adzapasuka, monga Salimani anapasula Betaribele; tsiku la nkhondo amai anaphwanyika pamodzi ndi ana ake.

15 Momwemo adzakuchitirani Betele, chifukwa cha choipa chanu chachikulu; mbandakucha mfumu ya Israele idzalikhika konse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/10-80907289bc518b6cde7deadba346282b.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 11

Kusayamika kwa Israele; machenjezo ndi malonjezo

1 Pamene Israele anali mwana, ndinamkonda, ndinaitana mwana wanga ali mu Ejipito.

2 Monga anawaitana, momwemo anawachokera; anaphera nsembe Abaala, nafukizira mafano osema.

3 Koma Ine ndinaphunzitsa Efuremu kuyenda, ndinawafungata m’manja mwanga; koma sanadziwe kuti ndinawachiritsa.

4 Ndinawakoka ndi zingwe za munthu, ndi zomangira za chikondi; ndinakhala nao ngati iwo akukweza goli pampuno pao, ndipo ndinawaikira chakudya.

5 Iye sadzabwerera kunka kudziko la Ejipito, koma Asiriya adzakhala mfumu yake, popeza anakana kubwera.

6 Ndi lupanga lidzagwera mizinda yake, lidzatha mipiringidzo yake, ndi kuononga chifukwa cha uphungu wao.

7 Ndipo anthu anga alimbika kubwerera m’mbuyo kundileka Ine; chinkana akawaitana atsate Iye ali m’mwamba, sadzakweza ndi mmodzi yense.

8 Ndidzakusiya bwanji, Efuremu? Ndidzakupereka bwanji, Israele? Ndidzakuyesa bwanji ngati Adima? Ndidzakuika bwanji ngati Zeboimu? Mtima wanga watembenuka m’kati mwanga, zachifundo zanga zilira zonse pamodzi.

9 Sindidzachita mkwiyo wanga waukali, sindidzabwerera kuononga Efuremu; pakuti Ine ndine Mulungu, si munthu ai; Woyera wa pakati pako; ndipo sindidzalowa m’mzinda.

10 Adzatsata Yehova, Iye adzabangula ngati mkango; pamene abangula, ana adzafika ndi kunjenjemera kuchokera kumadzulo.

11 Adzafika ndi kunjenjemera ngati mbalame ya ku Ejipito, ndi ngati nkhunda m’dziko la Asiriya; ndipo ndidzawakhalitsa m’nyumba zao, ati Yehova

12 Efuremu andizinga ndi bodza, ndi nyumba ya Israele ndi chinyengo, ndi Yuda apikisana ndi Mulungu, ndiye Woyera wokhulupirika.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/11-ceba3fb5fd7ce2456bce62a4af4cb393.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 12

Mlandu wa Yehova pa Israele ndi Yuda

1 Efuremu akudya mphepo, natsata mphepo ya kum’mawa; tsiku lonse achulukitsa mabodza ndi chipasuko, ndipo achita pangano ndi Asiriya, natenga mafuta kunka nao ku Ejipito.

2 Ndipo Yehova ali ndi mlandu ndi Yuda, nadzalanga Yakobo monga mwa njira zake, adzambwezera monga mwa machitidwe ake.

3 M’mimba anagwira kuchitendeni cha mkulu wake, ndipo atakula mphamvu analimbana ndi Mulungu;

4 inde, analimbana ndi wamthenga nampambana; analira, nampembedza Iye; anampeza Iye ku Betele, ndi kumeneko Iye analankhula ndi ife;

5 ndiye Yehova Mulungu wa makamu, chikumbukiro chake ndi Yehova.

6 M’mwemo utembenukire kwa Mulungu wako, sunga chifundo ndi chiweruzo, nuyembekezere Mulungu wako kosalekeza.

7 Ndiye Mkanani, m’dzanja lake muli miyeso yonyenga, akonda kusautsa.

8 Ndipo Efuremu anati, Zedi ndasanduka wolemera, ndadzionera chuma m’ntchito zonse ndinazigwira; sadzapeza mwa ine mphulupulu yokhala tchimo.

9 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wako chichokere dziko la Ejipito, ndidzakukhalitsanso m’mahema, monga masiku a zikondwerero zoikika.

10 Ndalankhulanso ndi aneneri, ndipo Ine ndachulukitsa masomphenya; ndi padzanja la aneneri ndinanena ndi mafanizo.

11 Kodi Giliyadi ndiye wopanda pake? Akhala achabe konse; mu Giligala aphera nsembe ya ng’ombe; inde maguwa ao a nsembe akunga miulu yamiyala m’michera ya munda.

12 Ndipo Yakobo anathawira kuthengo la Aramu, ndi Israele anagwira ntchito chifukwa cha mkazi, ndi chifukwa cha mkazi anaweta nkhosa.

13 Ndipo mwamneneriYehova anakweretsa Israele kuchokera mu Ejipito, ndi mwa mneneri anasungika.

14 Efuremu wautsa mkwiyo wowawa, m’mwemo Iye adzamsiyira mwazi wake, ndi Ambuye wake adzambwezera chomtonza chake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/12-a5247bf8c8d8ea87b7d0596d40ac0965.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 13

Tchimo la Israele ndi kulangidwa kwake

1 Pamene Efuremu analankhula panali kunjenjemera; anadzikweza mu Israele; koma pamene anapalamula mwaBaala, anafa.

2 Ndipo tsopano aonjeza kuchimwa, nadzipangira mafano oyenga asilivawao, mafano monga mwa nzeru zao, onsewo ntchito ya amisiri; anena za iwo, Anthu ophera nsembe apsompsone anaang’ombe.

3 Chifukwa chake adzakhala ngati mtambo wa m’mawa, ndi ngati mame akamuka mamawa, ngati mungu umene mphepo iuuluza kudwale, ndi ngati utsi wotuluka kukafwambira.

4 Koma Ine ndiye Yehova Mulungu wako chichokere m’dziko la Ejipito, ndipo suyenera kudziwa mulungu wina koma Ine; ndi popanda Ine palibe mpulumutsi.

5 Ndinakudziwa m’chipululu, m’dziko lotentha kwambiri.

6 Monga mwa podyetsa pao, momwemo anakhuta; anakhuta, ndi mtima wao unakwezeka; chifukwa chake anandiiwala Ine.

7 Chifukwa chake ndikhala nao ngati mkango; ngati nyalugwe ndidzalalira kunjira.

8 Ndidzakomana nao ngati chimbalangondo chochilanda ana ake, ndi kung’amba chokuta mtima wao; ndi pomwepo ndidzawalusira ngati mkango; chilombo chidzawamwetula.

9 Israele, chikuononga ndi ichi, chakuti utsutsana ndi Ine, chithandizo chako.

10 Ili kuti mfumu yako tsopano, kuti ikupulumutse m’mizinda yako yonse? Ndi oweruza ako amene unanena za iwo, Ndipatseni mfumu ndi akalonga?

11 Ndinakupatsa mfumu mu mkwiyo wanga; ndinamchotsanso mu ukali wanga.

12 Mphulupulu ya Efuremu yamangika, tchimo lake lisungika.

13 Zowawa zonga za mkazi wobala zidzamgwera, ndiye mwana wopanda nzeru; pakuti pali nyengo yakuti asachedwe mobalira ana.

14 Ndidzawaombola kumphamvu ya kumanda, ndidzawaombola kuimfa; imfa, miliri yako ili kuti? Kulekerera kudzabisika pamaso panga.

15 Chinkana abala mwa abale ake, mphepo ya kum’mawa idzafika, mphepo ya Yehova yokwera kuchokera kuchipululu; ndi gwero lake lidzaphwa, ndi kasupe wake adzauma, adzafunkha chuma cha akatundu onse ofunika.

16 Samariya adzasanduka wabwinja, pakuti anapandukana ndi Mulungu wake; iwo adzagwa ndi lupanga, ana ao amakanda adzaphwanyika, ndi akazi ao okhala ndi pakati adzatumbulidwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/13-aebf9218e58c9049adaf7d9c0c43f99f.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 14

Mulungu adandaulira Israele alape, nalonjeza kuwakhululukira

1 Israele, bwerera kunka kwa Yehova Mulungu wako; pakuti wagwa mwa mphulupulu yako.

2 Mukani nao mau, nimubwerere kwa Yehova; nenani kwa Iye, Chotsani mphulupulu zonse, nimulandire chokoma; ndipo tidzapereka mau milomo yathu ngati ng’ombe.

3 Asiriya sadzatipulumutsa; sitidzayenda pa akavalo, ndipo sitidzanenanso kwa ntchito ya manja athu, Inu ndinu milungu yathu; pakuti mwa Inu ana amasiye apeza chifundo.

4 Ndidzachiritsa kubwerera kwao, ndidzawakonda mwaufulu; pakuti mkwiyo wanga wamchokera.

5 Ndidzakhala kwa Israele ngati mame; adzachita maluwa ngati kakombo, ndi kutambalalitsa mizu yake ngati Lebanoni.

6 Nthambi zake zidzatambalala, ndi kukoma kwake kudzanga kwa mtengo waazitona, ndi fungo lake ngati Lebanoni.

7 Iwo okhala pansi pa mthunzi wake adzabwera, nadzatsitsimuka ngati tirigu, nadzaphuka ngati mpesa, chikumbukiro chake chidzanga vinyo wa Lebanoni.

8 Efuremu adzati, Ndili ndi chiyaninso ndi mafano? Ndayankha, ndidzampenyerera; ndili ngati mtengo wamlombwa wabiriwiri; zipatso zako zipezeka zochokera kwa Ine.

9 Wanzeru ndani, kuti azindikire izi? Waluntha, kuti adziwe izi? Pakuti njira za Yehova zili zoongoka; ndipo olungama adzayendamo, koma olakwa adzagwamo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/14-0bb80116005c4a009b21e41104698cc2.mp3?version_id=1068—