Categories
HOSEYA

HOSEYA Mau Oyamba

Mau Oyamba

Mneneri Hoseya adalalikira pambuyo pa mneneri Amosi, ku Israele, ufumu wakumpoto, mzinda wa Samariya usanapasuke. Iye amamva chisoni poona kuti Aisraelewo ngosakhulupirika ndi opembedza milungu ina. Tsono anayerekeza kusakhulupirika kwaoko ndi zimene mwiniwakeyo adazipeza m’banja lake, mkazi wake atamchokera nkutsata amuna ena. Chonchonso anthu a Mulunguwo anafulatira Yehova Mbuye wao natsata milungu ina. Mulungu sadzalephera kuwalanga chifukwa cha kusakhulupirika kwaoko; komabe potsiriza, chifukwa cha chikondi chake chosasinthika, adzawakokeranso kwa Iye ndipo adzayanjana nawonso. Atsimikiza chikondi chakecho ndi mauwa, “Ndidzakusiya bwanji, Efuremu? Ndidzakupereka bwanji, Israele…Mtima wanga watembenuka m’kati mwanga, zachifundo zanga zilira zonse pamodzi” (11.8).

Za mkatimu

Ukwati wa Hoseya ndi banja lake

1.1—3.5

Mau a Yehova odzudzula Israele

4.1—13.16

Uthenga wa kulapa ndinso lonjezo la kukonzedwanso kwa zinthu

14.1-9

Categories
HOSEYA

HOSEYA 1

Hoseya akwatira mkazi woipa kufanizira zoipa za Israele

1 Mau a Yehova amene anadza kwa Hoseya mwana wa Beeri masiku a Uziya, Yotamu, Ahazi, ndi Hezekiya, mafumu a Yuda, ndi masiku a Yerobowamu mwana wa Yowasi mfumu ya Israele.

2 Chiyambi cha kunena kwa Yehova mwa Hoseya. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, Muka, udzitengere mkazi wachigololo ndi ana achigololo; pakuti dziko latsata chigololo chokhachokha kuleka kutsata Yehova.

3 Ndipo anamuka natenga Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu; iye naima, nambalira mwana wamwamuna.

4 Ndipo Yehova anati kwa iye, Umutche dzina lake Yezireele; pakuti katsala kanthawi, ndipo ndidzabwezera chilango mwazi wa Yezireele pa nyumba ya Yehu, ndi kuleketsa ufumu wa nyumba ya Israele.

5 Ndipo kudzachitika tsiku lomwelo, ndidzathyola uta wa Israele m’chigwa cha Yezireele.

6 Ndipo anaimanso, nabala mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa iye, Umutche dzina lake Wosachitidwa-chifundo; pakuti sindidzachitiranso chifundo nyumba ya Israele, kuti ndiwakhululukire konse.

7 Koma ndidzachitira chifundo nyumba ya Yuda, ndi kuwapulumutsa mwa Ine Yehova Mulungu wao, osawapulumutsa ndi uta, kapena lupanga, kapena nkhondo ndi akavalo, kapena apakavalo.

8 Ataleka tsono kuyamwitsa Wosachitidwa-chifundo, anaima, nabala mwana wamwamuna.

9 Ndipo Yehova anati, Umutche dzina lake Si-anthu-anga; pakuti inu sindinu anthu anga, ndipo Ine sindine wanu.

Israele achitidwa chifundo

10 Angakhale anatero, kuwerenga kwake kwa ana a Israele kudzanga mchenga wa kunyanja, wosayeseka kapena kuwerengeka; ndipo kudzatero kuti m’mene adawanena, Simuli anthu anga, adzanena nao, Muli ana a Mulungu wamoyo.

11 Ndipo ana a Yuda ndi ana a Israele adzasonkhanidwa pamodzi, nadzadziikira mkulu mmodzi, nadzakwera kuchoka m’dziko; pakuti tsiku la Yezireele ndi lalikulu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/1-474d1109dd4267da8fd348ea812427af.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 2

1 Nenani kwa abale anu, Anthu anga, ndi kwa alongo anu, Wochitidwa-chifundo.

2 Mutsutsane naye mai wanu, mutsutsane naye; pakuti sali mkazi wanga, ndi Ine sindili mwamuna wake; ndipo achotse zadama zake pankhope pake, ndi zigololo zake pakati pa mawere ake;

3 ndingamvule wamaliseche, ndi kumuika ngati tsiku lija anabadwalo, ndi kumsanduliza ngati chipululu, ndi kumuika ngati dziko louma, ndi kumupha nalo ludzu;

4 ndipo ana ake sindidzawachitira chifundo; pakuti iwo ndiwo ana achigololo.

5 Pakuti mai wao anachita chigololo; iye amene anali ndi pakati pa iwo anachita chamanyazi; pakuti anati, Ndidzatsata ondikondawo, akundipatsa ine chakudya changa, ndi madzi anga, ubweya wanga, ndi thonje langa, mafuta anga, ndi chakumwa changa.

6 Chifukwa chake taonani, ndidzatchinga njira yako ndi minga, ndipo ndidzammangira mpanda, kuti asapeze mabande ake.

7 Ndipo adzatsata omkonda koma osawagwira, adzawafunafuna koma osawapeza; pamenepo adzati, Ndidzamuka ndi kubwererana ndi mwamuna wanga woyamba, popeza pamenepo panandikomera koposa tsopano.

8 Pakuti sanadziwe kuti ndine ndinampatsa tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi kumchulukitsirasilivandi golide, zimene anapanga nazoBaala.

9 Chifukwa chake ndidzabwera ndi kuchotsa tirigu wanga m’nyengo yake, ndi vinyo wanga m’nthawi yake yoikika, ndi kukwatula ubweya wanga ndi thonje langa, zimene zikadafunda umaliseche wake.

10 Ndipo tsopano ndidzaonetsa manyazi ake pamaso pa omkonda, popandanso wakumlanditsa m’dzanja langa.

11 Ndidzaleketsanso kusekerera kwake konse, zikondwerero zake, pokhala mwezi pake, ndimasabataake, ndi misonkhano yake yonse yoikika.

12 Ndipo ndidzapasula mipesa yake ndi mikuyu yake, imene adanena, Iyi ndi mphotho yanga anandipatsa ondikondawo; ndipo ndidzaisandutsa thengo, ndi nyama zakuthengo zidzaidya.

13 Ndipo ndidzamlanga chifukwa cha masiku a Abaala amene anawafukizira, navala mphete za m’mphuno, ndi zokometsera zake, natsata omkonda, nandiiwala Ine, ati Yehova.

14 Chifukwa chake taonani, ndidzamkopa ndi kunka naye kuchipululu, ndi kulankhula naye momkonda mtima.

15 Ndipo ndidzampatsa minda yake yampesa kuyambira pomwepo, ndi chigwa cha Akori chikhale khomo la chiyembekezo; ndipo adzavomereza pomwepo monga masiku a ubwana wake, ndi monga tsiku lokwera iye kutuluka m’dziko la Ejipito.

16 Ndipo kudzakhala tsiku lomwelo, ati Yehova, udzanditcha Mwamuna wanga, osanditchanso Baala wanga.

17 Pakuti ndidzachotsa maina a Abaala m’kamwa mwake; ndipo silidzakumbukikanso dzina lao.

18 Ndipo tsiku lomwelo ndidzawachitira pangano ndi nyama zakuthengo, ndi mbalame za mlengalenga, ndi zokwawa pansi; ndipo ndidzathyola uta, ndi lupanga, ndi nkhondo, zichoke m’dziko, ndi kuwagonetsa pansi mosatekeseka.

19 Ndipo ndidzakutomera ukhale wanga kosatha, inde ndidzakutomera ukhale wanga m’chilungamo, ndi m’chiweruzo, ndi mu ukoma mtima, ndi m’chifundo.

20 Ndidzakutomeranso ukhale wanga mokhulupirika, ndipo udzadziwa Yehova.

21 Ndipo kudzachitika tsiku lomwelo, ndidzavomereza, ati Yehova, ndidzavomereza thambo, ndi ilo lidzavomereza dziko lapansi;

22 ndi dziko lapansi lidzavomereza tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta; ndi izi zidzavomereza Yezireele.

23 Ndipo ndidzadzibzalira iye m’nthaka, ndipo ndidzachitira chifundo Wosachitidwa-chifundo; ndipo ndidzati kwa Si-anthu-anga, Muli anthu anga; ndipo iwo adzati, Ndinu Mulungu wathu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/2-d0827379effc90ec6a2ca243d99ab6a3.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 3

Akwatiranso mkazi woipa, kufaniziranso zochita ana a Israele

1 Ndipo Yehova anati kwa ine, Mukanso, konda mkazi wokondedwa ndi bwenzi lake, koma wakuchita chigololo, monga Yehova akonda ana a Israele, angakhale atembenukira kumilungu ina, nakonda nchinchi za mphesa zouma.

2 M’mwemo ndinadzigulira iye ndi masekeli khumi ndi asanu asiliva, ndi homeri ndi leteki wa barele;

3 ndipo ndinati kwa iye, Uzikhala ndi ine masiku ambiri, usachita chigololo, usakhala mkazi wa mwamuna aliyense; momwemo inenso nawe.

4 Pakuti ana a Israele adzakhala masiku ambiri opanda mfumu, ndi opanda kalonga, ndi opanda nsembe, ndi opanda choimiritsa, ndi opandaefodikapenaaterafi;

5 atatero ana a Israele adzabwera, nadzafuna Yehova Mulungu wao, ndi Davide mfumu yao, nadzafika ndi mantha kwa Yehova, ndi ku ukoma wake masiku otsiriza.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/3-4c3a9f43b001c991074188e26b2637e3.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 4

Mlandu pakati pa Mulungu ndi Israele

1 Imvani mau a Yehova, inu ana a Israele; pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi okhala m’dziko, popeza palibe choonadi, kapena chifundo, kapena kudziwa Mulungu m’dziko.

2 Koma kulumbira, ndi kunama, ndi kupha, ndi kuba, ndi kuchita chigololo; aboola, ndi mwazi ukhudzana nao mwazi.

3 Chifukwa chake dziko lidzachita chisoni, ndi aliyense wokhalamo adzalefuka, pamodzi ndi nyama zakuthengo, ndi mbalame za m’mlengalenga; ndi nsomba za m’nyanja zomwe zidzachotsedwa.

4 Koma munthu asatsutsane ndi mnzake, kapena kudzudzula mnzake; popeza anthu ako ndiwo akunga otsutsana ndi wansembe.

5 Ndipo udzakhumudwa usana, ndimneneriyemwe adzakhumudwa pamodzi ndi iwe usiku; ndipo ndidzaononga mai wako.

6 Anthu anga aonongeka chifukwa cha kusadziwa; popeza unakana kudziwa, Inenso ndikukaniza, kuti usakhale wansembe wanga; popeza waiwala chilamulo cha Mulungu wako, Inenso ndidzaiwala ana ako.

7 Monga anachuluka, momwemo anandichimwira; ndidzasanduliza ulemerero wao ukhale manyazi.

8 Adyerera tchimo la anthu anga, nakhumbira chosalungama chao, yense ndi mtima wake.

9 Ndipo kudzakhala monga anthu, momwemo wansembe; ndipo ndidzawalanga chifukwa chanjira zao, ndi kuwabwezera machitidwe ao.

10 Ndipo adzadya, koma osakhuta; adzachita chigololo, koma osachuluka; pakuti waleka kusamalira Yehova.

11 Chigololo, ndi vinyo, ndi vinyo watsopano, zichotsa mtima.

12 Anthu anga afunsira kumtengo wao, ndi ndodo yao iwafotokozera; pakuti mzimu wachigololo wawalakwitsa, ndipo achita chigololo kuchokera Mulungu wao.

13 Pamwamba pa mapiri aphera nsembe, nafukiza pazitunda, patsinde pa thundu, ndi minjali, ndi mkundi; popeza mthunzi wake ndi wabwino, chifukwa chake ana anu aakazi achita uhule, ndi apongozi anu achita chigololo.

14 Sindidzalanga ana anu aakazi pochita iwo uhule, kapena apongozi anu pochita chigololo iwo; pakuti iwo okha apatukira padera ndi akazi achiwerewere, naphera nsembe pamodzi ndi akazi operekedwa ku uhule; ndi anthu osazindikirawo adzagwetsedwa chamutu.

15 Chinkana iwe, Israele, uchita uhule, koma asapalamule Yuda; ndipo musafika inu ku Giligala, kapena kukwera ku Betaveni, kapena kulumbira, Pali Yehova.

16 Pakuti Israele wachita kuuma khosi ngati ng’ombe yaikazi yaing’ono youma khosi; tsopano Yehova adzawadyetsa ngatimwanawankhosakuthengo lalikulu.

17 Efuremu waphatikana ndi mafano, mlekeni.

18 Chakumwa chao chasasa, achita uhule kosalekeza; akulu ao akonda manyazi kwambiri.

19 Mphepo yamkulunga m’mapiko ake, ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zao.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/4-e9cbf51d18eb8fac295a99a21bf78333.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 5

Kulowerera kwa Israele

1 Imvani ichi, ansembe inu; mverani, inu nyumba ya Israele; tcherani khutu, inu nyumba ya mfumu; pakuti chiweruzochi chinena inu; pakuti munakhala msampha ku Mizipa, ndi ukonde woyalidwa pa Tabori.

2 Ndipo opandukawo analowadi m’zovunda; koma Ine ndine wakuwadzudzula onsewo.

3 Ndimdziwa Efuremu, ndi Israele sandibisikira; pakuti Efuremu iwe, wachita uhule tsopano, Israele wadetsedwa.

4 Machitidwe ao sawalola kubwerera kwa Mulungu wao; pakuti mzimu wa uhule uli m’kati mwao, ndipo sadziwa Yehova.

5 Ndipo kudzikuza kwa Israele kudzamchitira umboni pamaso pake; chifukwa chake Israele ndi Efuremu adzakhumudwa m’mphulupulu mwao; Yudanso adzakhumudwa pamodzi nao.

6 Adzamuka ndi zoweta zao zazing’ono ndi zazikulu kufunafuna Yehova: koma sadzampeza; Iye wadzibweza kuwachokera.

7 Anachita mosakhulupirika pa Yehova, pakuti anabala ana achilendo; mwezi wokhala udzawatha tsopano, pamodzi ndi maiko ao.

8 Ombani mphalasa mu Gibea, ndi lipenga mu Rama; fuulani ku Betaveni; pambuyo pako, Benjamini.

9 Efuremu adzasanduka bwinja tsiku lakudzudzula; mwa mafuko a Israele ndadziwitsa chodzachitikadi.

10 Akalonga a Yuda akunga anthu osuntha malire; ndidzawatsanulira mkwiyo wanga ngati madzi.

11 Efuremu azunzika, apsinjika pa mlanduwo; pakuti anafuna mwini wake kutsata lamulolo.

12 Ndipo ndikhala kwa Efuremu ngati njenjete, ndi kwa nyumba ya Yuda ngati chivundi.

13 Pamene Efuremu anaona nthenda yake, ndi Yuda bala lake, Efuremu anamuka kwa Asiriya, natumiza kwa mfumu Yarebu; koma iye sakhoza kukuchiritsani, kapena kupoletsa bala lanu.

14 Pakuti ndidzakhala kwa Efuremu ngati mkango, ndi kwa nyumba ya Yuda ngati msona wa mkango; ndidzamwetula Ine ndi kuchoka; ndidzanyamula, ndipo palibe wakulanditsa.

15 Ndidzamuka ndi kubwerera kunka kumalo kwanga, mpaka adzavomereza kupalamula kwao, nafunafuna nkhope yanga; m’msauko mwao adzandifunafuna mwachangu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/5-69ac92977b370130c45d0a23147dca4e.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 6

Israele abwerera kunka kwa Yehova

1 Tiyeni, tibwerere kunka kwa Yehova; pakuti wang’amba, nadzatipoletsera; wakantha, nadzatimanga.

2 Atapita masiku awiri adzatitsitsimutsa, tsiku lachitatu adzatiutsa; ndipo tidzakhala ndi moyo pamaso pake.

3 Tidziwe tsono, tilondole kudziwa Yehova; kutuluka kwake kwakonzekeratu ngati matanda kucha; ndipo adzatidzera ngati mvula, ngati mvula ya masika yakuthirira dziko.

Efuremu ndi Yuda adzudzulidwa

4 Efuremu iwe, ndidzakuchitira chiyani? Yuda iwe, ndikuchitire chiyani? Pakuti kukoma mtima kwako kukunga mtambo wam’mawa ndi ngati mame akuphawa mamawa.

5 Chifukwa chake ndawalikha mwa aneneri; ndawapha ndi mau a pakamwa panga; ndi maweruzo anga atuluka ngati kuunika.

6 Pakuti ndikondwera nacho chifundo, si nsembe ai; ndi kumdziwa Mulungu kuposa nsembe zopsereza.

7 Koma iwo analakwirachipanganongati Adamu, m’mene anandichitira monyenga.

8 Giliyadi ndiwo mzinda wa ochita zoipa, wa mapazi a mwazi.

9 Ndipo monga magulu a mbala alalira munthu, momwemo msonkhano wa ansembe amapha panjira ya ku Sekemu; indedi achita choipitsitsa.

10 M’nyumba ya Israele ndinaona chinthu choopsetsa; pamenepo pali uhule wa Efuremu; Israele wadetsedwa.

11 Akuikidwiratunso nyengo yakukolola, Yuda iwe, pamene ndikabwezanso undende wa anthu anga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/6-91f08a560cb7983efa0c21a59fae79af.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 7

Kuchimwa ndi kupandukira kwa Israele

1 M’mene ndichiritsa Israele, mphulupulu ya Efuremu ivumbuluka, ndi zoipa za Samariya; pakuti achita bodza, ndipo mkhungu alowa m’nyumba, ndi gulu la mbala lilanda kubwalo.

2 Ndipo sanena m’mtima mwao kuti Ine ndikumbukira zoipa zao zonse; tsopano machitidwe ao awazinga; ali pamaso panga.

3 Akondweretsa mfumu ndi zoipa zao, ndi akalonga ndi mabodza ao.

4 Achigololo onsewo; akunga ng’anjo anaitenthetsa wootcha mkate; aleka kusonkha moto, poyambira kukanda mtanda kufikira watupa mtandawo.

5 Tsiku la mfumu yathu akalonga adzidwalitsa ndi kutentha kwa vinyo; iye anatambasula dzanja lake pamodzi ndi oseka.

6 Pakuti asendera nao mtima wao wakunga ng’anjo ya mkate, pokhala alikulalira; wootcha mkate wao agona usiku wonse, m’mawa iyaka ngati moto wa malawi.

7 Onsewo atentha ngati ng’anjo, natha oweruza ao, agwa mafumu ao onse; palibe mmodzi mwa iwo wakuitana Ine.

8 Efuremu asokonezana nayo mitundu ya anthu; Efuremu ndiye kamtanda ka mkate kosatembenuzidwa.

9 Alendo anatha mphamvu yake osachidziwa iye; imvi zomwe zampakiza osachidziwa iye.

10 Ndipo kudzikuza kwa Israele kumchitira umboni pamaso pake; koma sanabwerere kunka kwa Yehova Mulungu wao, kapena kumfunafuna mwa ichi chonse.

11 Ndipo Efuremu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru; aitanira kwa Ejipito, amuka kwa Asiriya.

12 Pamene amuka ndidzawayalira ukonde wanga, ndidzawagwetsa ngati mbalame za m’mlengalenga, ndidzawalanga monga udamva msonkhano wao.

13 Tsoka kwa iwowa! Pakuti anandizembera; chionongeko kwa iwowa! Pakuti anandilakwira; ndikadawalanditsa Ine, koma anandinenera zabodza.

14 Ndipo sanafuulire kwa Ine ndi mtima wao, koma alira pakama pao, asonkhanira tirigu ndi vinyo, apikisana ndi Ine.

15 Chinkana ndawalangiza ndi lulimbitsa manja ao, andilingiririra choipa.

16 Abwerera, koma si kwa Wam’mwambayo; akunga uta wosakhulupirika; akalonga ao adzagwa ndi lupanga mwa chipongwe cha lilime lao; ichi ndicho adzawasekera m’dziko la Ejipito.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/7-edaf085e77dfdb97f19afedb5273129d.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 8

Kupembedza mafano ndi kusamvera kwa Israele

1 Lipenga kukamwa kwako. Akudza ngati chiombankhanga, kulimbana ndi nyumba ya Yehova; chifukwa analakwirachipanganochanga, napikisana nacho chilamulo changa.

2 Adzafuulira kwa Ine, Mulungu wanga, ife Aisraele tikudziwani.

3 Israele wachitaya chokoma, mdani adzamlondola.

4 Analonga mafumu, koma sikunachokera kwa Ine; anaika akalonga, koma sindinadziwa; anadzipangira mafano asilivawao ndi golide wao, kuti akalikhidwe.

5 Mwanawang’ombe wako wakutaya, Samariya iwe; mkwiyo wanga wayakira iwo; adzalephera kuyera mtima mpaka liti?

6 Pakuti ichi chomwe chafumira kwa Israele; mmisiri wampanga, koma sali Mulungu; inde mwanawang’ombe wa Samariya adzaphwanyikaphwanyika.

7 Pakuti abzala mphepo, nadzakolola kamvulumvulu; alibe tirigu wosasenga; ngala siidzatulutsa ufa; chinkana iutulutsa, alendo adzaumeza.

8 Israele wamezedwa; tsopano ali mwaamitundungati chotengera choti munthu sakondwera nacho.

9 Pakuti anakwera kunka ku Asiriya, ngati mbidzi ya pa yokha mwini wake; Efuremu walembera omkonda ngati antchito.

10 Inde angakhale alembera mwa amitundu ndidzawasonkhanitsa tsopano; ndipo ayamba kuchepa chifukwa cha katundu wa mfumu ya akalonga.

11 Popeza Efuremu anachulukitsa maguwa a nsembe akuchimwako, maguwa a nsembe omwewo anamchimwitsa.

12 Ndinamlembera zinthu zambirimbirizo za chilamulo changa, koma zinayesedwa ngati chinthu chachilendo.

13 Kunena za nsembe za zopereka zanga, aphera nsembe yanyama, naidya; koma Yehova sazilandira; tsopano adzakumbukira mphulupulu yao, nadzalanga zochimwa zao; adzabwerera kunka ku Ejipito.

14 Pakuti Israele waiwala Mlengi wake, namanga akachisi; ndipo Yuda wachulukitsa mizinda yamalinga; koma ndidzatumizira mizinda yake moto, nudzatha nyumba zake zazikulu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/8-18c048283f98cc4c860c68fe9ae69711.mp3?version_id=1068—

Categories
HOSEYA

HOSEYA 9

Tchimo la Israele ndi zotsatira zake

1 Usakondwera, Israele, ndi kusekerera, ngati mitundu ya anthu; pakuti wachita chigololo kuleka Mulungu wako, wakonda mphotho ya chigololo pa dwale la tirigu lililonse.

2 Dwale ndi choponderamo mphesa sizidzawadyetsa, vinyo watsopano adzamsowa.

3 Sadzakhala m’dziko la Yehova; koma Efuremu adzabwerera kunka ku Ejipito; ndipo adzadya chakudya chodetsa mu Asiriya.

4 Sadzatsanulira Yehova nsembe zavinyo; sizidzamkomera Iye nsembe zao; zidzakhala kwa iwo ngati mkate wa achisoni; onse akudyako adzadetsedwa; pakuti mkate wao udzakhala wa njala yao, uwu sudzalowa m’nyumba ya Yehova.

5 Mudzachitanji tsiku la misonkhano yoikika, ndi tsiku la chikondwerero cha Yehova.

6 Pakuti taonani, anachokera chionongeko, koma Ejipito adzawasonkhanitsa, Mofi adzawaika m’manda; khwisa adzalanda zofunika zao zasiliva; minga idzakhala m’mahema mwao.

7 Masiku a kulanga afika, masiku a kubwezera afika; Israele adzadziwa;mneneriali wopusa, munthu wamzimu ali wamisala, chifukwa cha kuchuluka mphulupulu yako, ndi popeza udani ndi waukulu.

8 Efuremu ndiye wozonda kwa Mulungu wanga; kunena za mneneri, msampha wa msodzi uli m’njira zake zonse, ndi udani m’nyumba ya Mulungu wake.

9 Anadzivunditsa kwambiri, monga masiku a Gibea; adzakumbukira mphulupulu yao, adzalanga zochimwa zao.

10 Ndinapeza Israele ngati mphesa m’chipululu, ndinaona makolo anu ngati chipatso choyamba cha mkuyu nyengo yake yoyamba; koma anadza kwa Baala-Peori, nadzipatulira chonyansacho, nasandulika onyansa, chonga chija anachikonda.

11 Kunena za Efuremu, ulemerero wao udzauluka ndi kuchoka ngati mbalame; sipadzakhala kubala, ndi kukhala ndi pakati, ndi kuima.

12 Angakhale alera ana ao, koma ndidzawasowetsa, wosatsala munthu; ndithunso tsoka iwowa, pamene ndiwachokera.

13 Efuremu, monga ndaona, akunga Tiro, wookedwa pokoma; koma Efuremu adzatulutsira ana ake wakuwaphera.

14 Apatseni, Yehova; mudzapatsa chiyani? Muwapatse mimba yotayataya, ndi mawere ouma.

15 Choipa chao chonse chili mu Giligala; pakuti pamenepo ndinawada, chifukwa cha kuipa kwa machitidwe ao ndidzawainga kuwachotsa m’nyumba mwanga; sindidzawakondanso; akalonga ao onse ndiwo opanduka.

16 Efuremu wakanthidwa, muzu wao wauma, iwo sadzabala zipatso; inde ngakhale abala, koma ndidzapha zipatso zofunika za mimba yao.

17 Mulungu wanga adzawataya, pakuti sanammvere Iye; ndipo adzakhala othawathawa mwaamitundu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HOS/9-5f1dd37c92c4b4258807946d52087f5f.mp3?version_id=1068—