Categories
HAGAI

HAGAI Mau Oyamba

Mau Oyamba

Mneneriyu adalalika mau ake chaka cha 520 BC., Ayuda ena atabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo. Anthuwo anali atabwerera ku ukapolo namakhala ku Yerusalemu kwa zaka zingapo, koma Kachisi anali bwinja lenileni. Atsogoleri anapereka uthenga kwa anthu kuti amangenso Kachisi, ndipo Ambuye akulonjeza kuti m’tsogolo anthu ake adzakhala pabwino ndi pa mtendere.

Za mkatimu

Yehova awalamula kuti amangenso Nyumba yake

1.1-15

Mau ena owalimbitsa mtima Ayudawo

2.1-23

Categories
HAGAI

HAGAI 1

Mau akudzudzula ndi kudandaulira Ayuda amangenso Kachisi

1 Chaka chachiwiri cha mfumu Dariusi, mwezi wachisanu ndi chimodzi, mau a Yehova anadza mwa Hagaimnenerikwa Zerubabele mwana wa Sealatiele, chiwanga cha Yuda, ndi kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kuti,

2 Atero Yehova wa makamu, akuti, Anthu awa anena, Nthawi siinafike, nthawi yakumanga nyumba ya Yehova.

3 Pamenepo mau a Yehova anadza mwa Hagai mneneri, ndi kuti,

4 Kodi imeneyi ndiyo nthawi yakuti inu nokha mukhala m’nyumba zanu zochingidwa m’katimo, ndi nyumba iyi ikhale yopasuka?

5 Chifukwa chake tsono, atero Yehova wa makamu: Mtima wanu usamalire njira zanu.

6 Mwabzala zambiri, koma mututa pang’ono; mukudya, koma osakhuta; mukumwa, koma osakoledwa; mudziveka, koma palibe wofundidwa; ndi iye wolembedwa ntchito yakulipidwa alandirira kulipirako m’thumba lobooka.

7 Atero Yehova wa makamu: Mtima wanu usamalire njira zanu.

8 Kwerani kudziko la mapiri, ndi kukwera nayo mitengo, nimumange nyumbayi; ndipo kudzandikomera, ndipo ndidzalemekezedwa, ati Yehova.

9 Munayembekezera zambiri, koma taonani, pang’ono; ndipo, mutabwera napo kwanu, ndinauzirapo. Chifukwa ninji? Ati Yehova wa makamu. Chifukwa cha nyumba yanga yokhala yopasuka, ndipo nuthamangira yense kunyumba kwake.

10 M’mwemo chifukwa cha inu kumwamba kukaniza mame, ndi nthaka ikaniza zipatso zake.

11 Ndipo ndinaitana chilala chidzere dziko, ndi mapiri, ndi tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi zimene ibala nthaka, ndi anthu, ndi zoweta, ndi ntchito zonse za manja.

12 Pamenepo Zerubabele mwana wa Sealatiele, ndi Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi otsala onse a anthu, anamvera mau a Yehova Mulungu wao, ndi mau a Hagai mneneri, monga Yehova Mulungu wao adamtuma; ndipo anthu anaopa pamaso pa Yehova.

13 Ndipo Hagai mthenga wa Yehova, mu uthenga wa Yehova ananena ndi anthu, ndi kuti, Ine ndili nanu, ati Yehova.

14 Ndipo Yehova anautsa mzimu wa Zerubabele mwana wa Sealatiele, chiwanga cha Yuda, ndi mzimu wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi mzimu wa otsala onse a anthu, ndipo anadza nagwira ntchito m’nyumba ya Yehova wa makamu, Mulungu wao,

15 tsiku la makumi awiri ndi anai la mwezi, mwezi wachisanu ndi chimodzi, chaka chachiwiri cha mfumu Dariusi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HAG/1-16890db4935bf58079d8e7fb62233cae.mp3?version_id=1068—

Categories
HAGAI

HAGAI 2

Ulemerero wa Kachisi wachiwiri

1 Mwezi wachisanu ndi chiwiri, tsiku la makumi awiri ndi chimodzi la mweziwo, mau a Yehova anadza mwa Hagaimneneri, ndi kuti,

2 Unenetu kwa Zerubabele, mwana wa Sealatiele, chiwanga cha Yuda, ndi kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa otsala a anthu, kuti,

3 Adatsala ndani mwa inu amene anaona nyumba iyi mu ulemerero wake woyamba? Ndipo muiona yotani tsopano? Kodi siikhala m’maso mwanu ngati chabe?

4 Koma limbika tsopano, Zerubabele, ati Yehova; ulimbikenso Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe; ndipo mulimbike inu nonse anthu a m’dziko, ati Yehova, ndi kuchita; pakuti Ine ndili pamodzi ndi inu, ati Yehova wa makamu;

5 monga momwe ndinapangana nanu muja munatuluka mu Ejipito, ndi Mzimu wanga unakhala pakati pa inu; musamaopa inu.

6 Pakuti atero Yehova wa makamu: Kamodzinso, katsala kanthawi, ndidzagwedeza miyamba ndi dziko lapansi, ndi nyanja, ndi mtunda womwe;

7 ndipo ndidzagwedezaamitunduonse, ndi zofunika za amitundu onse zidzafika, ndipo ndidzadzaza nyumba iyi ndi ulemerero, ati Yehova wa makamu.

8 Silivandi wanga, golide ndi wanga, ati Yehova wa makamu.

9 Ulemerero wotsiriza wa nyumba iyi udzaposa woyambawo, ati Yehova wa makamu; ndipo m’malo muno ndidzapatsa mtendere, ati Yehova wa makamu.

Madzudzulo ndi malonjezo

10 Tsiku la makumi awiri ndi anai la mwezi wachisanu ndi chinai, chaka chachiwiri cha Dariusi, mau a Yehova anadza mwa Hagai mneneri, ndi kuti,

11 Atero Yehova wa makamu: Funsatu ansembe za chilamulo, ndi kuti,

12 Munthu akanyamulira nyama yopatulika m’ngudulira, nakhudza mkate, kapena ndiwo, kapena vinyo, kapena mafuta, kapena chakudya chilichonse, ndi ngudulira, kodi chisandulika chopatulika? Ndipo ansembe anayankha nati, Iai.

13 Pamenepo Hagai anati, Munthu wodetsedwa ndi mtembo akakhudza kanthu ka izi, kodi kali kodetsedwa kanthuka? Ndipo ansembe anayankha nati, Kadzakhala kodetsedwa.

14 Ndipo Hagai anayankha, nati, Momwemo anthu awa, ndi momwemo mtundu uwu pamaso panga, ati Yehova; ndi momwemo ntchito iliyonse ya manja ao; ndi ichi achipereka, chili chodetsedwa.

15 Ndipo tsono, samalirani, kuyambira lero ndi m’tsogolomo, kuti, kusanaikidwe mwala pamwala mu Kachisi wa Yehova,

16 pamenepo ponse munthu akadza ku mulu woyenera miyeso makumi awiri, pali khumi yokha; munthu akadza ku choponderamo mphesa kudzatunga mbiya makumi asanu, pali makumi awiri okha.

17 Ndinakukanthani ndi chinsikwi ndi chinoni ndi matalala m’ntchito zonse za manja anu, koma simunabwerere kudza kwa Ine, ati Yehova.

18 Musamalire, kuyambira lero ndi m’tsogolo, kuyambira tsiku la makumi awiri ndi chinai la mwezi wachisanu ndi chinai, kuyambira tsiku lija anamanga maziko a Kachisi wa Yehova, samalirani.

19 Kodi mbeu ikali m’nkhokwe? Ngakhale mpesa, ndi mkuyu, ndi khangaza ndiazitonasizinabale; kuyambira lero lino ndidzakudalitsani.

Adani adzaonongeka, Zerubabele adzakwezeka

20 Ndipo mau a Yehova anadza nthawi yachiwiri kwa Hagai tsiku la makumi awiri la mwezi, ndi kuti,

21 Nena ndi Zerubabele chiwanga cha Yuda, kuti, Ndidzagwedeza miyamba ndi dziko lapansi;

22 ndipo ndidzagubuduza mipando yachifumu ya maufumu, ndidzaononga mphamvu ya maufumu a amitundu; ndidzagubuduza magaleta ndi iwo akuyendapo; ndi akavalo ndi apakavalo adzatsika, yense ndi lupanga la mbale wake.

23 Tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu, ndidzakutenga, Zerubabele mtumiki wanga, mwana wa Sealatiele, ati Yehova, ndi kuika iwe ngati mphete yosindikizira; pakuti ndakusankha, ati Yehova wa makamu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HAG/2-1d736c146f8a3d48f54df6f3d1e19fdb.mp3?version_id=1068—