Yosefe ammasulira Farao maloto ake
1 Ndipo panali zitapita zaka ziwiri zamphumphu,Faraoanalota; ndipo, taonani, anaima pamtsinje.
2 Ndipo, taonani, zinatuluka m’mtsinjemo ng’ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri za maonekedwe okoma ndi zonenepa; ndipo zinadya mabango.
3 Ndipo, taonani ng’ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zinatuluka m’mtsinjemo pambuyo pao, za maonekedwe oipa ndi zoonda; ndipo zinaima pa ng’ombe zinazo m’mphepete mwa mtsinje.
4 Ndipo ng’ombe zazikazi za maonekedwe oipa ndi zoonda zinadya ng’ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri za maonekedwe abwino ndi zonenepazo. Ndipo Farao anauka.
5 Ndipo anagona nalotanso kachiwiri; ndipo taonani, ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zinamera pa mbuwa imodzi, zonenepa ndi zabwino.
6 Ndipo, taonani, ngala zisanu ndi ziwiri, zoonda zopserera ndi mphepo ya kum’mawa, zinamera pambuyo pao.
7 Ndipo ngala zoondazo zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zonenepa ndi zodzalazo. Ndipo Farao anauka, ndipo, taonani, analota.
8 Ndipo panali m’mamawa mtima wake unavutidwa; ndipo anatumiza naitana amatsenga onse a mu Ejipito, ndi anzeru onse a momwemo: ndipo Farao anafotokozera iwo loto lake; koma panalibe mmodzi anakhoza kuwamasulira iwo kwa Farao.
9 Pamenepo wopereka chikho wamkulu anati kwa Farao, kuti, Ine ndidzakumbukira zochimwa zanga lero.
10 Farao anakwiya ndi anyamata ake, nandiika ine ndisungidwe m’nyumba ya kazembe wa alonda, ine ndi wophika mkate wamkulu:
11 ndipo tinalota loto usiku umodzi ine ndi iye; tinalota munthu yense monga mwa kumasulira kwa loto lake.
12 Ndipo panali ndi ife mnyamata Muhebri, kapolo wa kazembe wa alonda, ndipo ife tinafotokozera iye, ndipo iye anatimasulira ife maloto athu; kwa munthu yense monga loto lake anatimasulira.
13 Ndipo panali monga momwe iye anatimasulira, momwemo mudachitika; ine anandibwezera mu utumiki wanga, mnzanga anampachika.
14 Ndipo Farao anatumiza nakaitana Yosefe; ndipo anamtulutsa iye msanga m’dzenjemo: ndipo iye anameta, nasintha malaya ake, nalowa kwa Farao.
15 Farao ndipo anati kwa Yosefe, Ine ndalota loto, koma palibe wondimasulira; ndipo ndamva alikunena za iwe kuti, ukamva loto udziwa kumasulira.
16 Ndipo Yosefe anayankha Farao kuti, Si mwa ine; koma Mulungu adzayankha Farao mwamtendere.
17 Ndipo Farao ananena kwa Yosefe, M’loto langa taona, ndinaima m’mphepete mwa mtsinje;
18 ndipo taona, zinatuluka m’mtsinjemo ng’ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri, zonenepa ndi za maonekedwe abwino; ndipo zinadya m’mabango;
19 ndipo taona, ng’ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zina zinatuluka pambuyo pao zosauka ndi za maonekedwe oipa ndi zoonda, zoipa zotere sindinazione m’dziko la Ejipito;
20 ndipo ng’ombe zazikazi zoonda ndi za maonekedwe oipa zinadya ng’ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zonenepa.
21 Ndipo pamene zinadya sizinadziwike kuti zinadya; koma zinaipabe m’maonekedwe ao monga poyamba.
22 Pamenepo ndinauka. Ndipo ndinaona m’kulota kwanga, taona, ngala zisanu ndi ziwiri zinamera pa mbuwa imodzi zodzala ndi zabwino;
23 ndipo, taona, ngala zisanu ndi ziwiri zina zofota, zoonda, zopserera ndi mphepo ya kum’mawa, zinamera pambuyo pao;
24 ndipo ngala zoonda zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zabwino; ndipo ndinafotokozera amatsenga: koma panalibe wondimasulira ine.
25 Ndipo Yosefe anati kwa Farao, Loto la Farao lili limodzi: chimene Mulungu ati achite wam’masulira Farao.
26 Ng’ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zabwino ndizo zaka zisanu ndi ziwiri, ndi ngala zisanu ndi ziwiri zabwino ndizo zaka zisanu ndi ziwiri: loto lili limodzi.
27 Ng’ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zoonda ndi za maonekedwe oipa zinatuluka pambuyo pao ndizo zaka zisanu ndi ziwiri, ndiponso ngala zisanu ndi ziwiri zopanda kanthu zopserera ndi mphepo ya kum’mawa, ndizo zaka zisanu ndi ziwiri za njala.
28 Ichi ndi chinthu chimene ndinena kwa Farao: chimene Mulungu ati achite wasonyeza kwa Farao.
29 Taonani, zidzafika zaka zisanu ndi ziwiri zakuchuluka chakudya m’dziko lonse la Ejipito;
30 ndipo pambuyo pao zidzauka zaka zisanu ndi ziwiri za njala; ndipo anthu adzaiwala zochuluka zonsezo m’dziko la Ejipito; ndipo njala idzapululutsa dziko;
31 ndipo zochuluka sizidzazindikirika chifukwa cha njala ikudza m’mbuyoyo, pakuti idzavuta.
32 Ndipo lotolo linabwerezedwa kawiri kwa Farao, chifukwa chinthu chili chokhazikika ndi Mulungu, ndipo Mulungu afulumira kuchichita.
33 Tsopano, Farao afunefune munthu wakuzindikira ndi wanzeru, amkhazike iye ayang’anire dziko la Ejipito.
34 Farao achite chotere, alembe woyang’anira dziko wosonkhetsa limodzi la magawo asanu la dziko la Ejipito m’zaka zisanu ndi ziwiri zakuchuluka dzinthu.
35 Iwo asonkhanitse chakudya chonse cha zaka zabwino izo zilinkudzazo, aunjike tirigu m’manja a Farao akhale chakudya m’mizinda, namsunge.
36 Ndipo chakudyacho chidzakhala m’dziko chosonkhera zaka zisanu ndi ziwiri za njala imene idzakhala m’dziko la Ejipito; kuti dziko lisaonongedwe ndi njala.
Yosefe wolamulira dziko la Ejipito
37 Ndipo chinthucho chinali chabwino m’maso mwa Farao, ndi m’maso mwa anyamata ake.
38 Ndipo Farao anati kwa anyamata ake, Kodi ife tidzaone munthu ngati uyu, mzimu wa Mulungu uli m’mtima mwake?
39 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Popeza Mulungu wakuonetsa iwe zonsezo palibe wina wakuzindikira ndi wanzeru ngati iwe.
40 Uziyang’anira pa nyumba yanga, ndipo anthu anga onse adzalamulidwa mwa mau ako; pa mpando wachifumu pokha ine ndidzakuposa iwe.
41 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Taona, ndakhazika iwe wolamulira dziko lonse la Ejipito.
42 Ndipo Farao anachotsa mphete yosindikizira yake padzanja lake, naiveka padzanja la Yosefe, namveka iye ndi zovalira zabafuta, naika unyolo wagolide pakhosi pake;
43 ndipo anamkweza iye m’galeta wake wachiwiri amene anali naye: ndipo anafuula patsogolo pa iye, Gwadani; ndipo anamkhazika iye wolamulira dziko lonse la Ejipito.
44 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Ine ndine Farao, ndipo popanda iwe palibe munthu aliyense adzatukula dzanja lake kapena mwendo wake m’dziko lonse la Ejipito.
45 Ndipo Farao anamutcha dzina la Yosefe Zafenati-Panea; ndipo anampatsa akwatire Asenati mwana wamkazi wa Potifera wansembe wa Oni. Ndipo Yosefe anatuluka wolamulira, nayendayenda m’dziko la Ejipito.
46 Ndipo Yosefe anali wa zaka makumi atatu pamene iye anaima pamaso pa Farao mfumu ya Aejipito. Ndipo Yosefe anatuluka pamaso pa Farao, napitapita padziko lonse la Ejipito.
47 Ndipo zaka zisanu ndi ziwiri zakuchuluka dzinthu nthaka inabala zambirimbiri.
48 Ndipo anasonkhanitsa chakudya chonse cha zaka zisanu ndi ziwiri chimene chinali m’dziko la Ejipito, nasunga chakudyacho m’mizinda; chakudya cha m’minda, yozinga mizinda yonse, anachisunga m’menemo.
49 Ndipo Yosefe anasunga tirigu ngati mchenga wa panyanja, wambirimbiri kufikira analeka kuwerenga; chifukwa anali wosawerengeka.
50 Ndipo kwa Yosefe anabadwa ana aamuna awiri, chisanafike chaka cha njala, amene Asenati mwana wamkazi wa Potifera wansembe wa Oni anambalira iye.
51 Ndipo Yosefe anamutcha dzina la woyamba Manase, chifukwa anati iye, Mulungu wandiiwalitsa ine zovuta zanga zonse, ndi nyumba yonse ya atate wanga.
52 Ndipo dzina la wachiwiri anamutcha Efuremu: chifukwa Mulungu anandibalitsa ine m’dziko la kusauka kwanga.
53 Ndipo zaka zakuchuluka dzinthu zisanu ndi ziwiri za m’dziko la Ejipito, zinatha.
54 Ndipo zinayamba kufika zaka zisanu ndi ziwiri za njala, monga ananena Yosefe; ndipo munali njala m’maiko monse; koma m’dziko lonse la Ejipito munali chakudya.
55 Ndipo pamene dziko lonse la Ejipito linali ndi njala, anthu anafuulira Farao awapatse chakudya; ndipo Farao anati kwa Aejipito onse, Pitani kwa Yosefe: chimene iye anena kwa inu chitani.
56 Ndipo njala inali padziko lonse lapansi; ndipo Yosefe anatsegula nkhokwe zonse nagulitsa Aejipito: ndipo njala inakula m’dziko la Ejipito.
57 Ndipo maiko onse anafika ku Ejipito kudzagula tirigu kwa Yosefe: chifukwa njala inakula m’dziko lonse lapansi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GEN/41-21583131850d3c27433a9cb9de2da4f7.mp3?version_id=1068—