Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 10

Masomphenya a akerubi

1 Ndipo ndinapenya, ndipo taonani, kuthambo lokhala pamwamba pa mitu yaakerubikudaoneka ngati mwala wasafiro, ngati maonekedwe a chifaniziro cha mpando wachifumu pamwamba pao.

2 Ndipo Yehova analankhula ndi munthu wovala bafuta, nati, Lowa pakati pa njingazi pansi pa kerubi, nudzaze manja ako makala a moto ochokera pakati pa akerubi, nuwamwaze pamwamba pa mzinda. Nalowa, ndili chipenyere ine.

3 Tsono akerubi anaima kudzanja lamanja la nyumba polowa munthuyo, ndi mtambo unadzaza bwalo la m’kati.

4 Ndipo ulemerero wa Yehova unakwera kuchokera kukerubi kunka kuchiundo cha nyumba; ndi nyumba inadzala nao mtambo, ndi bwalo linadzala ndi cheza cha ulemerero wa Yehova.

5 Ndipo mkokomo wa mapiko a akerubi unamveka mpaka bwalo lakunja, ngati mau a Mulungu Wamphamvuyonse, pakunena Iye.

6 Ndipo kunali pomlamulira munthu wovala bafutayo, ndi kuti, Para moto pakati pa njingazi ndi pakati pa akerubi; iye analowa, naima m’mbali mwa njinga.

7 Pamenepo kerubi wina anatambasula dzanja lake pakati pa akerubi kumoto uli pakati pa akerubi, napalako, nauika m’manja mwa iye wovala bafuta, ndiye naulandira, natuluka.

8 Ndipo panaoneka pa akerubi chonga dzanja la munthu pansi pa mapiko ao.

9 Pamenepo ndinapenya, ndipo taonani, njinga zinai m’mbali mwa akerubi, njinga imodzi m’mbali mwa kerubi mmodzi, ndi njinga ina m’mbali mwa kerubi wina, ndi maonekedwe a njingazi ananga mawalidwe a berulo.

10 Ndipo maonekedwe ake, zonse zinai zinafanana, ngati njinga ziwiri zopingasitsana.

11 Pakuyenda akerubi anayenda kumbali zao zinai, sanatembenuke poyenda; koma komwe udalozako mutu anatsatako, sanatembenuke poyenda.

12 Ndipo thupi lao lonse, ndi misana yao, ndi manja ao, ndi mapiko ao, ndi njinga zomwe, zinadzala ndi maso pozungulira pao, zingakhale njingazi anai aja anali nazo.

13 Kunena za njingazi, wina anazifuulira, ndili chimvere ine, Kunkhulirani.

14 Ndipo aliyense anali nazo nkhope zinai, nkhope yoyamba ndiyo nkhope ya kerubi, ndi nkhope yachiwiri ndiyo nkhope ya munthu, ndi yachitatu ndiyo nkhope ya mkango, ndi yachinai ndiyo nkhope ya chiombankhanga.

15 Pamenepo akerubi anakwera, ndizo zamoyo zija ndinaziona kumtsinje Kebara.

16 Ndipo pakuyenda akerubi, njinga zinayenda pambali pao, ndi pakutambasula mapiko ao akerubiwo kuuluka padziko, njingazi sizinatembenuke pambali pao.

17 Pakuima iwo zinaima izi, ndi pakukwera iwo izi zinakwera pamodzi nao; pakuti mzimu wa zamoyozo unali mwa izo.

18 Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiundo cha nyumba, nuima pamwamba pa akerubi.

19 Ndipo akerubi anatambasula mapiko ao, nauluka padziko, ndili chipenyere, pakuchoka iwo ndi njingazi pa mbali pao; ndipo anaima pa chitseko cha chipata cha kum’mawa cha nyumba ya Yehova, ndi ulemerero wa Mulungu wa Israele unali pamwamba pao.

20 Awa ndi zamoyozo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israele kumtsinje Kebara, ndipo ndinadziwa kuti ndiwo akerubi.

21 Yense anali nazo nkhope zinai, ndi yense mapiko anai, ndi chifaniziro cha manja a munthu pansi pa mapiko ao.

22 Ndi chifaniziro cha nkhope zao ndicho nkhope zomwezo ndinaziona kumtsinje Kebara, maonekedwe ao ndi iwo eni; aliyense anayenda, nalunjika m’tsogolo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/10-d459c63013bae8a7fe7fc5cf88dcf3da.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 11

Chiweruzo cha Mulungu pa mafumu a Ayuda

1 Pamenepo unandikweza mzimu, nudza nane kuchipata cha kum’mawa cha nyumba ya Yehova choloza kum’mawa; ndipo taonani, pa chitseko cha chipata amuna makumi awiri mphambu asanu; ndipo ndinaona pakati pao Yazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya, akalonga a anthu.

2 Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, awa ndi anthu olingirira za mphulupulu, ndi kupangira uphungu woipa m’mzinda muno;

3 ndiwo akuti, siinafike nyengo yakumanga nyumba; mzinda uwu ndi mphika, ife ndife nyama.

4 Chifukwa chake uwanenere, neneratu, wobadwa ndi munthu iwe.

5 Pamenepo mzimu wa Yehova unandigwera, ndipo anati kwa ine, Nena, Atero Yehova, Mwatero nyumba ya Israele, pakuti ndidziwa zimene zimalowa m’mtima mwanu.

6 Mwachulukitsa ophedwa anu m’mzinda muno, mwadzazanso makwalala ake ndi ophedwawo.

7 Chifukwa chake atero Yehova Mulungu, Ophedwa anu munawaika m’kati mwake, iwo ndiwo nyama imene, ndi mzinda uwu ndiwo mphika; koma inu mudzatulutsidwa m’kati mwake.

8 Mwaopa lupanga, tsono ndidzakufikitsirani lupanga, ati Yehova Mulungu.

9 Ndipo ndidzakutulutsani m’kati mwake, ndi kukuperekani m’manja a alendo, ndi kuchita maweruzo pakati panu.

10 Mudzagwa ndi lupanga, ndidzakuweruzirani kumalire a Israele; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

11 Mzinda uno sudzakhala mphika wanu, ndi inu simudzakhala nyama m’kati mwake, ndidzakuweruzirani kumalire a Israele;

12 ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pakuti simunayende m’malemba anga, kapena kuchita maweruzo anga, koma mwachita monga mwa maweruzo aamitunduokhala pozungulira panu.

13 Ndipo kunali, pakunenera ine, anamwalira Pelatiya mwana wa Benaya. Pamenepo ndinagwa nkhope yanga pansi, ndi kufuula ndi mau aakulu, ndi kuti, Kalanga ine, Yehova Mulungu? Mudzatsiriza kodi otsala a Israele?

14 Ndipo mau a Yehova anandidzera kuti,

15 Wobadwa ndi munthu iwe, abale ako, inde abale ako aamuna a chibale chako, ndi nyumba yonse ya Israele, yonseyi ndiwo amene okhala muYerusalemuananena nao, Muzikhala kutali kwa Yehova; dziko ili lapatsidwa kwa ife, likhale cholowa chathu;

16 chifukwa chake uziti, Atero Yehova Mulungu, Ngakhale ndawachotsa kutali mwa amitundu, ngakhalenso ndawabalalikitsa m’maiko, koma ndidzawakhalira malo opatulika kanthawi kumaiko adafikako.

17 Chifukwa chake uziti, Atero Yehova Mulungu, Ndidzakumemezani kumitundu ya anthu, ndi kukusonkhanitsani muchoke m’maiko m’mene munabalalikiramo, ndipo ndidzakuninkhani dziko la Israele.

18 Ndipo adzafikako, nadzachotsako zonyansa zake zonse, ndi zake zonse zakuipitsamo.

19 Ndipo ndidzawapatsa mtima umodzi, ndi kuika mzimu watsopano m’kati mwao; ndipo ndidzawachotsera mtima wamwala m’thupi mwao, ndi kuwapatsa mtima wamnofu;

20 kuti ayende m’malemba anga, ndi kusunga maweruzo anga, ndi kuwachita; ndipo adzakhala anthu anga, ndi Ine ndidzakhala Mulungu wao.

21 Koma iwo amene mtima wao unatsata mtima wa zonyansa zao, ndi zoipitsitsa zao, ndidzawabwezera njira yao pamutu pao, ati Yehova Mulungu.

22 Pamenepoakerubianatambasula mapiko ao, ndi njinga zinali pa mbali pao; ndi ulemerero wa Mulungu wa Israele unali pamwamba pao.

23 Ndipo ulemerero wa Yehova unakwera kuchoka pakati pa mzinda, nuima paphiri la kum’mawa kwa mzinda.

24 Ndipo mzimu unandikweza, nufika nane m’masomphenya mwa mzimu wa Mulungu kudziko la Ababiloni, kwa andendewo. M’mwemo masomphenya ndidawaona anandichokera, nakwera.

25 Pamenepo ndinanena ndi andendewo zonse zija adandionetsa Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/11-cbb910feacce70f66beedaa88604a47b.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 12

Khoma labooledwa lofanizira ukapolo ndi ubalaliko wao

1 Mau a Yehova anandidzeranso, ndi kuti,

2 Wobadwa ndi munthu iwe, ukhala pakati pa nyumba yampanduko, yokhala nao maso akuonera, koma osaona; ndi makutu akumvera, koma osamva; pakuti iwo ndiwo nyumba yampanduko.

3 Potero wobadwa ndi munthu iwe, udzikonzeretu akatundu a pa ulendo wa kundende, nuchoke usana pamaso pao, uchoke pokhala iwepo kunka malo ena pamaso pao; kapena adzachizindikira, angakhale ndiwo nyumba yopanduka.

4 Uzitulutsa akatundu ako usana pamaso pao, ngati a pa ulendo wa kundende; ndipo madzulo uzituluka wekha pamaso pao, monga amatuluka olowa kundende.

5 Udziboolere khoma pamaso pao, nuwatulutsire akatundu pamenepo.

6 Pamaso pao uwasenze paphewa pako, ndi kuwatulutsa kuli mdima, nuphimbe nkhope yako kuti usapenye dziko; popeza ndakuika chizindikiro cha nyumba ya Israele.

7 Ndipo ndinachita monga momwe anandilamulira, ndinatulutsa akatundu anga usana, ngati a pa ulendo wa kundende, ndi madzulo ndinaboola pakhoma ndi dzanja langa, ndinawatulutsa pali mdima, ndi kuwasenza paphewa panga pamaso pao.

8 Ndipo m’mawa mau a Yehova anandidzera, ndi kuti,

9 Wobadwa ndi munthu iwe, kodi nyumba ya Israele, nyumba yampanduko, siinati kwa iwe, Uchitanji?

10 Unene nao, Atero Ambuye Yehova, Katundu uyu anena za kalonga wa muYerusalemu, ndi nyumba yonse ya Israele yokhala pakati pao.

11 Uziti, Ine ndine chizindikiro chanu, monga ndachita ine momwemo kudzachitidwa nao; adzachotsedwa kunka kundende.

12 Kalongayo ali pakati pao adzasenza paphewa pake mumdima, nadzatuluka; adzaboola palinga, nadzatulutsapo; adzaphimba nkhope yake kuti asapenye dziko ndi maso ake.

13 Ndidzamphimba ndi ukonde wanga, nadzakodwa iye mu msampha wanga; ndipo ndidzafika naye ku Babiloni, ku dziko la Ababiloni; sadzaliona, chinkana adzafako.

14 Ndipo onse omzinga kumthandiza, ndi magulu ake onse, ndidzawamwaza kumphepo zonse, ndidzawasololeranso lupanga lakuwatsata.

15 Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pakuwamwaza Ine mwaamitundu, ndi kuwabalalitsa m’maiko.

16 Koma ndidzawasiya owerengeka apulumuke lupanga, ndi njala, ndi mliri, kuti afotokoze zonyansa zao kwa amitundu kumene afikako; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

17 Anandidzeranso mau a Yehova, akuti,

18 Wobadwa ndi munthu iwe, udye mkate wako ndi kunthunthumira, ndi kumwa madzi ako ndi kunjenjemera, ndi kutenga nkhawa;

19 nunene kwa anthu a m’dziko, Atero Yehova Mulungu za iwo okhala mu Yerusalemu, ndi za dziko la Israele, Adzadya mkate wao ndi nkhawa, ndi kumwa madzi ao ndi kusumwa; pakuti dziko lao lidzakhala lachipululu, kuleka kudzala kwake chifukwa cha chiwawa cha onse okhalamo.

20 Ndi mizinda yokhalamo anthu idzapasuka, ndi dziko lidzakhala labwinja; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

Aneneratu kutsutsa aneneri onama

21 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

22 Wobadwa ndi munthu iwe, ngwotani mwambi umene muli nao m’dziko la Israele, wakuti, Masiku achuluka, ndi masomphenya ali onse apita pachabe?

23 Chifukwa chake unene nao, Atero Yehova Mulungu, Ndidzaleketsa mwambi uwu, ndipo sadzautchulanso mwambi mu Israele; koma unene nao, Masiku ayandikira, nadzachitika masomphenya ali onse.

24 Pakuti sikudzakhalanso masomphenya achabe, kapena ula wosyasyalika m’nyumba ya Israele.

25 Pakuti Ine ndine Yehova, ndidzanena, ndi mau ndidzanenawo adzachitika, osazengerezekanso; pakuti m’masiku anu, nyumba yopanduka inu, ndidzanena mau ndi kuwachita, ati Yehova Mulungu.

26 Anandidzeranso mau a Yehova, akuti,

27 Wobadwa ndi munthu iwe, taona, iwo a nyumba ya Israele akuti, masomphenya awaona ndiwo a masiku ambiri; ndipo anenera za nthawi zili kutali.

28 Chifukwa chake uziti nao, Atero Ambuye Yehova, Palibe amodzi a mau anga adzazengerezekanso; koma mau ndidzanenawo adzachitika, ati Ambuye Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/12-f748c86ff27bd295330b9a89b3c5537e.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 13

1 Ndipo mau a Yehova anandidzera ine, akuti,

2 Wobadwa ndi munthu iwe, Unenere za aneneri a Israele onenerawo, nuziti nao onenera za m’mtima mwaomwao, Tamverani mau a Yehova.

3 Atero Ambuye Yehova, Tsoka aneneri opusawo akutsata mzimu waowao, chinkana sanaone kanthu.

4 Aneneri ako, Israele, akhala ngati nkhandwe m’mapululu.

5 Simunakwera kuima mopasuka, kapena kumanganso linga la nyumba ya Israele, kuima kunkhondo tsiku la Yehova.

6 Iwo aona zopanda pake, ndi phenda labodza amene anena, Atero Yehova; koma Yehova sanawatume, nayembekezetsa anthu kuti mauwo adzakhazikika.

7 Simunaona masomphenya opanda pake kodi? Simunanena ula wabodza kodi? Pakunena inu, Atero Yehova; chinkana sindinanene?

8 Chifukwa chake atero Ambuye Yehova, Popeza mwanena zopanda pake, ndi kuona mabodza, chifukwa chake taonani, ndikhala Ine wotsutsana nanu, ati Ambuye Yehova.

9 Ndi dzanja langa lidzakhala lotsutsana nao aneneri akuona zopanda pake, ndi kupenda za bodza; sadzakhala mu msonkhano wa anthu anga, kapena kulembedwa m’buku lolembedwamo nyumba ya Israele; kapena kulowa m’dziko la Israele; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

10 Popeza, inde popeza asokeretsa anthu anga, ndi kuti, Mtendere, pokhala palibe mtendere; ndipo anthu akamanga linga, aneneriwo alimata ndi dothi losapondeka;

11 uziti nao olimata ndi dothi losapondeka, kuti lidzagwa, lidzavumbidwa ndi mvula yaikulu; ndi inu, matalala aakulu, mudzagwa; ndi mkuntho udzalithithimula.

12 Ndipo taonani, litagwa linga, sadzanena nanu kodi, Lili kuti dothi munalimata nalo?

13 Chifukwa chake atero Ambuye Yehova, Ndidzalithithimula ndi mkuntho mu ukali wanga; ndipo lidzavumbidwa ndi mvula yaikulu mu mkwiyo wanga, ndi matalala aakulu adzalitha mu ukali wanga.

14 M’mwemo ndidzagumula linga munalimata ndi dothi losapondeka, ndi kuligwetsa pansi; kuti maziko ake agadabuke, ndipo lidzagwa; ndi inu mudzathedwa pakati pake; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

15 M’mwemo ndidzakwaniritsa ukali wanga pa lingalo, ndi pa iwo analimata ndi dothi losapondeka, ndipo ndidzati kwa inu, Lingalo palibe, ndi olimata palibe,

16 ndiwo aneneri a Israele akunenera zaYerusalemu, nauonera masomphenya a mtendere, pamene palibe mtendere, ati Ambuye Yehova.

Mau akutsutsa aneneri aakazi onama

17 Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, uziika nkhope yako itsutsane nao ana aakazi a anthu ako, akunenera za m’mtima mwao, nunenere chowatsutsa,

18 nuziti, Atero Ambuye Yehova, Tsoka akazi osoka zophimbira mfundo zonse za dzanja, ndi iwo okonza zokuta mitu za misinkhu iliyonse, kuti asake miyoyo! Kodi musaka miyoyo ya anthu anga ndi kudzisungira miyoyo yanu?

19 Ndipo mundidetsa mwa anthu anga kulandirapo barele wodzala manja, ndi zidutsu za mkate, kuipha miyoyo yosayenera kufa, ndi kusunga miyoyo yosayenera kukhala ndi moyo, ndi kunena mabodza kwa anthu anga omvera bodza.

20 Chifukwa chake atero Ambuye Yehova, Taonani, nditsutsana nazo zophimbira zanu, zimene musaka nazo miyoyo komweko, kuiuluza; ndipo ndidzazikwatula m’manja mwanu, ndi kuimasula, ndiyo miyoyo muisaka kuiuluza.

21 Zokuta mitu zanu zomwe ndidzazing’amba, ndi kulanditsa anthu anga m’manja mwanu; ndipo sadzakhalanso m’mphamvu mwanu kusakidwa; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

22 Popeza mwamvetsa chisoni ndi mabodza mtima wa wolungama, amene sindinamvetse chisoni Ine, ndi kumlimbitsa manja woipa, kuti asabwerere kuleka njira yake yoipa, ndi kusungidwa wamoyo;

23 chifukwa chake simudzaonanso zopanda pake, kapena kupenda; koma ndidzalanditsa anthu anga m’manja mwanu; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/13-6321c0ed8fb48e646b0e9cb037dd8592.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 14

Chilango cha pa opembedza mafano

1 Pamenepo anafika kwa ine akulu ena a Israele nakhala pansi pamaso panga.

2 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

3 Wobadwa ndi munthu iwe, anthu awa anautsa mafano ao mumtima mwao, naimika chokhumudwitsa cha mphulupulu yao pamaso pao; ndifunsidwe nao konse kodi?

4 Chifukwa chake ulankhule nao, nunene nao, Atero Ambuye Yehova, Aliyense wa nyumba ya Israele wakuutsa mafano ake mumtima mwake, naimika chokhumudwitsa cha mphulupulu yake pamaso pake, nadza kwamneneri, Ine Yehova ndidzamyankhapo monga mwa mafano ake aunyinji;

5 kuti ndigwire nyumba ya Israele mumtima mwao; popeza onsewo asanduka alendo ndi Ine mwa mafano ao.

6 Chifukwa chake uziti kwa nyumba ya Israele, Atero Ambuye Yehova, Bwerani, lekani mafano anu, tembenuzani nkhope zanu kuzisiya zonyansa zanu zonse.

7 Pakuti aliyense wa nyumba ya Israele, kapena wa alendo ogonera mu Israele, wodzisiyanitsa kusatsata Ine, nautsa mafano ake m’mtima mwake, naimika chokhumudwitsa cha mphulupulu yake pamaso pake, nadzera mneneri kudzifunsira kwa Ine, Ine Yehova ndidzamyankha ndekha;

8 ndipo ndidzaikira munthu uyu nkhope yanga imtsutse, ndi kumuyesa chodabwitsa, ndi chizindikiro, ndi mwambi, ndi kumsadza pakati pa anthu anga; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9 Ndipo akacheteka mneneriyo, nakanena mau, Ine Yehova ndamcheta mneneri uja; ndipo ndidzamtambasulira dzanja langa, ndi kumuononga pakati pa anthu anga Israele.

10 Ndipo adzasenza mphulupulu yao, mphulupulu ya mneneri idzanga mphulupulu ya uja wamfunsira;

11 kuti nyumba ya Israele isasocherenso kusatsata Ine, kapena kudzidetsanso ndi zolakwa zao zonse; koma kuti akhale anthu anga, ndipo ndikhale Ine Mulungu wao, ati Ambuye Yehova.

Malango a Mulungu ali olungama

12 Ndipo anandidzera mau a Yehova akuti,

13 Likandichimwira dziko ndi kuchita monyenga, ndipo ndikalitambasulira dzanja langa, ndi kulithyolera mchirikizo wake, ndiwo mkate, ndi kulitumizira njala, ndi kulidulira munthu ndi nyama,

14 chinkana akadakhala m’mwemo anthu awa atatu, Nowa, Daniele, ndi Yobu, akadapulumutsa moyo wao wokha mwa chilungamo chao, ati Ambuye Yehova.

15 Ndikapititsa zilombo zoipa pakati padziko, ndi kupulula ana, kuti likhale lachipululu losapitako munthu chifukwa cha zilombo,

16 chinkana anthu omwewo atatu akadakhala m’mwemo, Pali Ine, ati Ambuye Yehova, sakadapulumutsa ana aamuna kapena aakazi; iwo akadapulumuka okha; koma dziko likadakhala lachipululu.

17 Kapena ndikadza padziko ndi lupanga, ndi kuti, Lupanga lipite pakati padziko, kuti ndilidulire munthu ndi nyama;

18 chinkana anthu atatuwo akadakhala m’mwemo, Pali Ine, ati Ambuye Yehova, sakadapulumutsa ana aamuna kapena aakazi; koma iwo akadapulumuka okha.

19 Kapena ndikatumizira dzikolo mliri, ndi kulitsanulira ukali wanga ndi mwazi, kulidulira munthu ndi nyama;

20 chinkana Nowa, Daniele, ndi Yobu, akadakhala m’mwemo, Pali Ine, ati Ambuye Yehova, sakadapulumutsa ana aamuna kapena aakazi; akadapulumutsa moyo wao wokha ndi chilungamo chao.

21 Pakuti atero Ambuye Yehova, Kopambana kotani nanga ndikatumiziraYerusalemumaweruzo anga anai owawa, lupanga, njala, zilombo zoipa, ndi mliri, kuudulira anthu ndi nyama?

22 Koma onani mudzatsala opulumuka m’mwemo amene adzatulutsidwa, ndiwo ana aamuna ndi aakazi; taonani, adzatuluka kudza kwa inu; ndipo mudzaona njira zao, ndi zochita zao; mudzatonthozedwanso pa zoipa ndazitengera pa Yerusalemu, inde pa zonse ndazitengerapo.

23 Ndipo adzakusangalatsani pamene muona njira yao, ndi zochita zao; ndipo mudzadziwa kuti sindinazichite kopanda chifukwa zonse ndinazichita momwemo, ati Ambuye Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/14-ee8961a8876891ea583c9964907bdafd.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 15

Mtengo wopanda pake

1 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

2 Wobadwa ndi munthu iwe, mtengo wampesa uposeranji mtengo uliwonse wina, nthambi ya mpesa yokhalayo mwa mitengo ya kunkhalango?

3 Kodi atengako mtengo kupanga nao ntchito? Atengako chichiri kodi kupachikapo chipangizo chilichonse?

4 Taona, auponya kumoto kuuyesa nkhuni, moto unyeketsa nsonga zake zonse ziwiri, nupserera pakati pake, kodi ukomera ntchito iliyonse?

5 Taonani, pokhala wamphumphu sunayenere ntchito iliyonse, nanga utanyeketsa moto nupserera udzayeneranso ntchito iliyonse?

6 Chifukwa chake atero Ambuye Yehova, Ngati mtengo wampesa pakati pa mitengo ya kunkhalango ndauponya kumoto ukhale nkhuni, momwemo ndidzapereka okhala muYerusalemu.

7 Ndipo ndidzaika nkhope yanga iwatsutse; adzatuluka kumoto, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pakuika Ine nkhope yanga iwatsutse.

8 Ndipo ndidzasandutsa dziko chipululu; popeza anachita cholakwa, ati Ambuye Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/15-b6e0b7a88321e34c615468447e6b148d.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 16

Kusakhulupirika kwa Yerusalemu

1 Anandidzeranso mau a Yehova, akuti,

2 Wobadwa ndi munthu iwe, DziwitsaYerusalemuzonyansa zake, nuziti,

3 Atero Ambuye Yehova kwa Yerusalemu, Chiyambi chako ndi kubadwa kwako ndiko kudziko la Akanani; atate wako anali Mwamori, ndi mai wako Muhiti.

4 Ndipo za kubadwa kwako, tsiku lobadwa iwe sanadule nchofu yako, sanakuyeretse ndi kukusambitsa ndi madzi, sanakuthire mchere konse, kapena kukukulunga m’nsalu ai.

5 Panalibe diso linakuchitira chifundo, kukuchitira chimodzi chonse cha izi, kuchitira iwe nsoni; koma unatayidwa kuyere; pakuti ananyansidwa nao moyo wako tsiku la kubadwa kwako.

6 Ndipo popita Ine panali iwepo, ndinakuona ulikuvimvinizika m’mwazi mwako. Pamenepo ndinanena ndi iwe m’mwazi wako. Khala ndi moyo, inde ndinati kwa iwe m’mwazi mwako, Khala ndi moyo.

7 Ndinakuchulukitsa ngati mphundu za kumunda; ndipo unathululuka ndi kukula kufikira wakongola nkhope, mawere ako anamera, ndi tsitsi lako linamera; koma unali wamaliseche ndi wausiwa.

8 Ndipo popita Ine panali iwepo ndi kukupenya, taona nyengo yako ndiyo nyengo yakukondana; pamenepo ndinakufunda chofunda changa, ndi kuphimba umaliseche wako; inde ndinakulumbirira ndi kupangana nawe, ati Ambuye Yehova, ndipo unakhala wanga.

9 Ndipo ndinakusambitsa ndi madzi, inde ndinakutsuka kukuchotsera mwazi wako, ndi kukudzoza mafuta.

10 Ndinakuvekanso ndi nsalu zopikapika, ndi kukuveka nsapato za chikopa cha katumbu; ndinakuzenenga nsalu yabafuta, ndi kukuphimba ndi nsalu yasilika.

11 Ndinakukometseranso ndi zokometsera, ndi kuika zigwinjiri m’manja mwako, ndi unyolo m’khosi mwako.

12 Momwemo ndinaika chipini m’mphuno mwako, ndi maperere m’makutu mwako, ndi korona wokongola pamutu pako.

13 Ndipo unadzikometsera ndi golide, ndisiliva, ndi chovala chako ndi bafuta ndi silika ndi yopikapika; unadya ufa wosalala, ndi uchi, ndi mafuta; ndipo unali wokongola woposa ndithu, ndipo unapindulapindula kufikira unasanduka ufumu.

14 Ndi mbiri yako inabuka mwaamitunduchifukwa cha kukongola kwako; pakuti ndiko kwangwiro, mwa ulemerero wanga ndinauika pa iwe, ati Ambuye Yehova.

15 Koma unatama kukongola kwako, ndi kuchita zachigololo potama mbiri yako, ndi kutsanulira zigololo zako pa munthu aliyense wopitapo; unali wake.

16 Ndipo unatengako zovala zako, ndi kudzimangira misanje ya mawangamawanga, ndi kuchitapo chigololo; zotere sizinayenere kufika kapena kuchitika.

17 Unatenganso zokometsera zako zokoma za golide wanga ndi siliva wanga, zimene ndinakupatsa, ndi kudzipangira mafano a amuna, ndi kuchita nao chigololo.

18 Unatenganso zovala zako za nsalu yopikapika, ndi kuwaveka nazo, unaikanso mafuta anga ndi chofukiza changa pamaso pao.

19 Ndi mkate wanga ndinakupatsawo, ufa wosalala, ndi mafuta, ndi uchi, ndinakudyetsazo, unawaikira izi pamaso pao, zichite fungo lokoma; kunatero, ati Ambuye Yehova.

20 Unatenganso ana ako aamuna ndi aakazi amene unandibalirawo, ndi kuwapereka nsembe awathe. Zigololo zako zidachepa kodi,

21 kuti unawapha ana anga ndi kuwapereka, pakuwapititsa pamoto?

22 Ndipo pa zonyansa zako zonse ndi zigololo zako sunakumbukire masiku a ubwana wako, muja unakhala wamaliseche ndi wausiwa, womvimvinizika m’mwazi wako.

23 Ndipo kudachitika utatha zoipa zako zonse, (tsoka iwe, tsoka, ati Ambuye Yehova)

24 unadzimangira nyumba yachimphuli, unadzimangiranso chiunda m’makwalala ali onse.

25 Unamanga chiunda chako pa mphambano zilizonse, ndipo unanyansitsa kukongola kwako, ndi kutukula mapazi ako kwa yense wopitako, ndi kuchulukitsa chigololo chako.

26 Wachitanso chigololo ndi Ejipito oyandikizana nawe, aakulu thupi, ndi kuchulukitsa chigololo chako kuutsa mkwiyo wanga.

27 Taona tsono, ndakutambasulira dzanja langa, ndi kuchepsa gawo lako la chakudya, ndi kukupereka ku chifuniro cha iwo akudana nawe, kwa ana aakazi a Afilisti akuchita manyazi ndi njira yako yoipa.

28 Unachitanso chigololo ndi Aasiriya, pakuti unakhala wosakoledwa, inde unachita chigololo nao, koma sunakoledwe.

29 Unachulukitsanso chigololo chako m’dziko la Kanani, mpaka dziko la Ababiloni, koma sunakoledwe nachonso.

30 Ha? Mtima wako ngwofooka, ati Ambuye Yehova, pakuchita iwe izi zonse, ndizo ntchito za mkazi wachigololo wouma m’maso.

31 Pakumanga nyumba yako yachimphuli pa mphambano zilizonse, ndi pomanga chiunda chako m’makwalala ali onse, sunakhale ngati mkazi wadama waphindu, popeza unapeputsa mphotho.

32 Ndiwe mkazi wokwatibwa wochita chigololo, wolandira alendo m’malo mwa mwamuna wake.

33 Anthu amaninkha akazi onse achigololo mphatso, koma iwe umaninkha mabwenzi ako onse mphatso zako ndi kuwalipira, kuti akudzere kuchokera kumbali zonse, kuti achite nawe chigololo.

34 M’mwemo usiyana konse ndi akazi ena m’chigololo chako; pakuti palibe wokutsata kuchita nawe chigololo; popezanso uwalipira, koma sakupatsa iwe mphotho; potero usiyana nao konse ena.

35 Chifukwa chake, wachigololo iwe, tamvera mau a Yehova:

36 Atero Ambuye Yehova, Popeza ndalama zako zamwazika, nuvundukuka umaliseche wako mwa chigololo chako ndi mabwenzi ako, ndi chifukwa cha mafano onse a zonyansa zako, ndi mwazi wa ana ako umene unawapatsa;

37 chifukwa chake taona, ndidzasonkhanitsa mabwenzi ako onse amene wakondwera nao, ndi onse unawakonda, pamodzi ndi onse unawada; inde ndidzawasonkhanitsira iwe pozungulira ponse, ndi kuwavundukulira umaliseche wako, kuti aone umaliseche wako wonse.

38 Ndipo ndidzaweruza mlandu wako, monga aweruza akazi achigololo ndi okhetsa mwazi; ndipo ndidzakutengera mwazi wa ukali ndi wa nsanje.

39 Ndidzakuperekanso m’dzanja lao, ndipo adzagwetsa nyumba yako yachimphuli, ndi kugumula ziunda zako, nadzakuvula zovala zako, ndi kulanda zokometsera zako zokongola, nadzakusiya wamaliseche ndi wausiwa.

40 Ndipo adzamemezera iwe msonkhano, nadzakuponya miyala, ndi kukupyoza ndi malupanga ao.

41 Ndipo adzatentha nyumba zako ndi moto, nadzakuweruza pamaso pa akazi ambiri; ndipo ndidzakuleketsa kuchita chigololo, ndipo sudzalipiranso mphotho yachigololo.

42 M’mwemo ukali wanga udzakhuta nawe, ndi nsanje yanga idzakuchokera, ndipo ndidzakhala chete wosakwiyanso.

43 Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako, koma wandivuta nazo zonsezi, chifukwa chake taona, Inenso ndidzakubwezera njira yako pamutu pako, ati Ambuye Yehova; ndipo sudzachita choipa ichi choonjezerapo pa zonyansa zako zonse.

44 Taona, aliyense wonena miyambi adzakunenera mwambi uwu, wakuti, Monga make momwemo mwana wake.

45 Iwe ndiwe mwana wa mai ako wonyansidwa naye mwamuna wake ndi ana ake, ndipo iwe ndiwe mng’ono wao wa akulu ako akunyansidwa ndi amuna ao ndi ana ao; mai wako ndiye Muhiti, ndi atate wako ndiye Mwamori.

46 Ndi mkulu wako ndiye Samariya, wokhala kudzanja lako lamanzere, iye ndi ana ake aakazi; ndi mng’ono wako wokhala kudzanja lako lamanja ndiye Sodomu ndi ana ake aakazi.

47 Koma sunayende m’njira zao, kapena kuchita monga mwa zonyansa zao pang’ono pokha; unawaposa iwo m’kuvunda kwako, m’njira zako zonse.

48 Pali Ine, ati Ambuye Yehova, Sodomu mng’ono wako sanachite, iye kapena ana ake aakazi, monga umo unachitira iwe ndi ana ako aakazi.

49 Taona, mphulupulu ya mng’ono wako Sodomu ndi iye, kudzikuza, kuchuluka kwa chakudya, ndi kupumula kwa mtambasali, anali nako iye ndi ana ake; ndipo sanalimbitse dzanja la wosauka ndi wosowa.

50 Ndipo anadzikuza, nachita chonyansa pamaso panga; chifukwa chake ndinawachotsa pakuchiona.

51 Ngakhale Samariya sanachite theka la zochimwa zako, koma unachulukitsa zonyansa zako, kuwaposa iwowa, ndi kuika abale ako olungama ndi zonyansa zako zonse unazichita.

52 Usenzenso manyazi ako, iwe wakuweruza abale ako mwa zochimwa zako unazichita monyansa koposa iwowa; iwo akuposa iwe m’chilungamo chao, nawenso uchite manyazi nusenze manyazi ako, popeza waika abale ako olungama.

53 Ndipo ndidzabweza undende wao, undende wa Sodomu ndi ana ake, ndi undende wa Samariya ndi ana ake, ndi undende wa andende ako pakati pao;

54 kuti usenze manyazi ako, ndi kuti uchite manyazi chifukwa cha zonse unazichita pakuwatonthoza.

55 Ndipo abale ako Sodomu ndi ana ake adzabwerera umo unakhalira kale, ndipo Samariya ndi ana ake adzabwerera umo anakhalira kale; ndi iwe ndi ana ako mudzabwerera umo munakhalira kale.

56 Ndipo sunakambe za mbale wako Sodomu pakamwa pako tsiku la kudzikuza kwako;

57 chisanavundukuke choipa chako monga nthawi ya chitonzo cha ana aakazi a Aramu, ndi onse akumzungulira iye, ana aakazi a Afilisti akupeputsa pozungulira ponse.

58 Wasenza choipa chako ndi zonyansa zako, ati Yehova.

59 Pakuti atero Ambuye Yehova, Ndidzachita ndi iwe monga umo unachitira; popeza wapepula lumbiro ndi kuthyola pangano.

60 Koma ndidzakumbukira Ine pangano langa ndi iwe m’masiku a ubwana wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha nawe.

61 Pamenepo udzakumbukira njira zako ndi kuchita manyazi, pakulandira abale ako aakulu ndi aang’ono; ndipo ndidzakupatsa awa akhale ana ako aakazi, angakhale sali a pangano lako.

62 Pakuti ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova;

63 kuti uzikumbukira ndi kuchita manyazi ndi kusatsegulanso pakamwa pako konse, chifukwa chamanyazi ako, pamene ndikufafanizira zonse unazichita, ati Ambuye Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/16-5266d6ae848f35c0213b9d16ba11a56b.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 17

Fanizo la ziombankhanga ziwiri ndi mpesa

1 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

2 Wobadwa ndi munthu iwe, ipha mwambi, nunene fanizo kwa nyumba ya Israele,

3 nuziti, Atero Ambuye Yehova, Chiombankhanga chachikulu ndi mapiko aakulu, ndi maphiphi aatali, odzala nthenga cha mathothomathotho, chinafika ku Lebanoni, nkutenga nsonga ya mkungudza,

4 chinabudula nsonga yosomphoka ya nthambi zake zanthete, ndi kumuka nayo kudziko la malonda, chinaiika m’mzinda wa amalonda.

5 Chinatengakonso mbeu ya m’dziko, ndi kuibzala m’nthaka yokoma, chinaiika panali madzi ambiri, chinaioka ngati mtengo wamsondodzi.

6 Ndipo inaphuka, nikhala mpesa wotambalala waufupi msinkhu, nthambi zake zinapindikira momwe, ndi mizu yake pansi pake, nikhala mpesa, nuonetsa nthambi ndi kuphuka mphukira.

7 Panalinso chiombankhanga china chachikulu, ndi mapiko aakulu, ndi nthenga zambiri; ndipo taona, mpesa uwu unachipindira mizu yake, nuchilunjikitsira zake, kuchokera pookedwa pake, kuti chiuthirire madzi.

8 Unaokedwa mu nthaka yabwino kuli madzi ambiri, kuti uphuke nthambi, nubale zipatso, nukhale mpesa wabwino.

9 Uziti, Atero Ambuye Yehova, Udzakondwa kodi? Sadzausula ndi kudula zipatso zake, kuti uume, kuti masamba ake onse ophuka aume, ngakhale palibe mphamvu yaikulu, kapena anthu ambiri akuuzula?

10 Inde ungakhale waokedwa udzakondwa kodi? Sudzauma chiumire kodi pakuuomba mphepo ya kum’mawa? Udzauma pookedwa apo udaphuka.

11 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti.

12 Uziti, tsono kwa nyumba ya mpandukoyi, Simudziwa kodi izi nchiyani? Uziti, Taonani mfumu ya ku Babiloni inadza kuYerusalemu, nkutenga mfumu yake ndi akalonga ake, nkubwera nao kuli iye ku Babiloni;

13 ndipo inatenga wa mbumba yachifumu, nkuchita naye pangano, nkumlumbiritsa, nkuchotsa amphamvu a m’dziko;

14 kuti ufumuwo ukhale wopepuka, kuti usadzikweze, koma kuti pakusunga pangano lake ukhale.

15 Koma anapandukira ndi kutuma mithenga yake ku Ejipito, kuti ampatse akavalo ndi anthu ambiri. Adzapindula kodi? Adzapulumuka wakuchita izi? Athyole pangano ndi kupulumuka kodi?

16 Pali Ine, ati Ambuye Yehova, pamalo pokhala mfumu, imene idamchititsa ufumu, imene anapeputsa lumbiro lake, imene anathyola pangano lake, adzafa pamodzi ndi iye pakati pa Babiloni.

17 NdipoFaraondi nkhondo yake yaikulu, ndi khamu lake launyinji, sadzachita pamodzi naye kunkhondo, pakuunda mtumbira, ndi kumanga malinga, kulikha anthu ambiri.

18 Pakuti anapepula lumbiro, ndi kuthyola pangano, angakhale anapereka dzanja lake; popeza anachita izi zonse sadzapulumuka.

19 Chifukwa chake atero Ambuye Yehova, Pali Ine, lumbiro langa, analipepula, ndi pangano langa analithyola, ndidzawabweza pamutu pake.

20 Ndidzamphimbanso ndi ukonde wanga, nadzakodwa iye mu msampha wanga; ndipo ndidzadza naye ku Babiloni, ndi kunena naye komweko mlandu wa kulakwa kwake anandilakwira nako.

21 Ndipo othawa ake onse m’magulu ake onse adzagwa ndi lupanga, ndi otsala adzabalalitsidwa kumphepo zonse; ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndanena.

22 Atero Ambuye Yehova, Ndidzatenganso nsonga ya mkungudza wautali ndi kuiika; ndidzabudula nsonga yosomphoka ya nthambi zake zanthete, ndi kuioka paphiri lalitali lothuvuka;

23 paphiri lothuvuka la Israele ndidzaioka, ndipo idzaphuka nthambi ndi kubala zipatso, nidzakhala mkungudza wokoma, ndi m’munsi mwake mudzakhala mbalame zilizonse za mapiko aliwonse; mu mthunzi wa nthambi zake zidzabindikira.

24 Ndipo mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine Yehova ndatsitsa mtengo wosomphoka, ndakuza mtengo waung’ono, ndaumitsa mtengo wauwisi, ndi kuphukitsa mtengo wouma; Ine Yehova ndanena ndi kuchichita.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/17-8990e2855f87d8f3c387aac6418261f3.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 18

Udindo ndi wakewake wa munthu

1 Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

2 Mutani inu ndi kunena mwambi uwu za dziko la Israele, wakuti, Atate adadya mphesa zosacha, ndi mano a ana ayayamira.

3 Pali Ine, ati Ambuye Yehova, simudzaonanso chifukwa cha kunena mwambiwu mu Israele.

4 Taonani, miyoyo yonse ndi yanga, monga moyo wa atate momwemonso moyo wa mwana, ndiyo yanga; moyo wochimwawo ndiwo udzafa.

5 Koma munthu akakhala wolungama, nakachita chiweruzo ndi chilungamo,

6 wosadya pamapiripo, wosakweza maso ake kumafano a nyumba ya Israele, wosaipsa mkazi wa mnansi wake, kapena kuyandikira mkazi ataoloka,

7 wosasautsa munthu aliyense, koma wambwezera wangongole chigwiriro chake, wosatenga zofunkha, anampatsa wanjala chakudya chake, naveka wamaliseche ndi chovala,

8 wosapereka molira phindu, wosatenga choonjezerapo wobweza dzanja lake lisachite chosalungama, woweruza zoona pakati pa munthu ndi mnzake,

9 amayenda m’malemba anga, nasunga maweruzo anga kuchita chokhulupirika; iye ndiye wolungama, adzakhala ndi moyo ndithu, anena Ambuye Yehova.

10 Akabala mwana ndiye mkhungu, wokhetsa mwazi, wochita chimodzi cha izi,

11 wosachita zabwino zonse zija, koma anadyanso pamapiri, naipsa mkazi wa mnansi wake,

12 nasautsa osauka ndi osowa, natenga zofunkha, wosabwezera chigwiriro, nakweza maso ake kumafano, nachita chonyansa,

13 napereka molira phindu, nalandira choonjezerapo; adzakhala ndi moyo uyu kodi? Sadzakhala ndi moyo, anachita zonyansa izi zonse; kufa adzafadi, mwazi wake umkhalira.

14 Taona tsono, yemweyo akabala mwana uyu, naona zochimwa zonse adazichita atate wake, naopa wosachita zoterezo,

15 wosadya pamapiri, kapena kukweza maso ake kumafano a nyumba ya Israele, wosaipsa mkazi wa mnansi wake,

16 kapena kusautsa wina aliyense, wosatenga chigwiriro, wosatenga zofunkha; koma anapatsa wanjala chakudya chake, naveka wamaliseche ndi chovala,

17 naletsa dzanja lake pa wozunzika, wosalandira phindu kapena choonjezerapo, wochita maweruzo anga, nayenda m’malemba anga; uyu sadzafera mphulupulu ya atate wake, adzakhala ndi moyo ndithu.

18 Atate wake, popeza anazunza chizunzire, nafunkha za mbale wake, nachita chimene sichili chabwino pakati pa anthu ake, taona, adzafa mu mphulupulu yake.

19 Koma inu mukuti, Alekeranji mwana kusenza mphulupulu za atate wake? Mwanayo akachita chiweruzo ndi chilungamo, nakasunga malemba anga onse, ndi kuwachita, adzakhala ndi moyo ndithu.

20 Moyo wochimwawo ndiwo udzafa; mwana sadzasenza mphulupulu za atate wake, ndi atate sadzasenza mphulupulu za mwana; chilungamo cha wolungama chidzamkhalira, ndi choipa cha woipa chidzamkhalira,

21 Koma woipayo akabwerera kusiya machimo ake onse adawachita nakasunga malemba anga onse, ndi kuchita chiweruzo ndi chilungamo, adzakhala ndi moyo ndithu, sadzafa.

22 Nnena chimodzi chonse cha zolakwa zake zonse adazichita chidzakumbukika chimtsutse; m’chilungamo chake adachichita adakhala ndi moyo.

23 Ngati ndikondwera nayo imfa ya woipa? Ati Ambuye Yehova, si ndiko kuti abwerere kuleka njira yake, ndi kukhala ndi moyo?

24 Koma wolungamayo akabwerera kuleka chilungamo chake, nakachita mphulupulu, ndi kuchita monga mwa zonyansa zonse azichita woipa, adzakhala ndi moyo kodi? Nnena chimodzi cha zolungama zake zonse adzazichita chidzakumbukika m’kulakwa kwake analakwa nako, ndi m’kuchimwa kwake anachimwa nako; momwemo adzafa.

25 Koma mukuti, Njira ya Ambuye njosayenera. Tamvera tsono nyumba ya Israele, Kodi njira yanga njosayenera? Njira zanu si ndizo zosayenera?

26 Wolungamayo akatembenukira kuleka chilungamo chake, nakachita mphulupulu, adzafa momwemo; m’mphulupulu yake adaichita adzafa.

27 Ndipo woipayo akatembenukira kuleka choipa chake adachichita, nakachita chiweruzo ndi chilungamo, adzapulumutsa moyo wake.

28 Popeza anasamalira, natembenukira kuleka zolakwa zake zonse adazichita, adzakhala ndi moyo ndithu, sadzafa.

29 Koma nyumba ya Israele imanena, Njira ya Ambuye njosayenera. Inu, nyumba ya Israele, kodi njira zanga nzosayenera? Njira zanu si ndizo zosayenera?

30 Chifukwa chake ndidzakuweruzani inu, nyumba ya Israele, yense monga mwa njira zake, ati Ambuye Yehova. Bwererani, nimutembenukire kuleka zolakwa zanu zonse, ndipo simudzakhumudwa nazo, ndi kuonongeka nayo mphulupulu.

31 Tayani, ndi kudzichotsera zolakwa zanu zonse zimene munalakwa nazo, ndi kudzifunira mtima watsopano, ndi mzimu watsopano; pakuti mudzaferanji inu, nyumba ya Israele?

32 Pakuti sindikondwera nayo imfa ya wakufayo, ati Ambuye Yehova; chifukwa chake bwererani, nimukhale ndi moyo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/18-0ada652a499ae2f94e22320e83a43101.mp3?version_id=1068—

Categories
EZEKIELE

EZEKIELE 19

Fanizo la mkango waukazi, ndi la mpesa

1 Ndipo iwe, takwezera akalonga a Israele nyimbo ya maliro,

2 uziti, Mai wako ndi chiyani? Mkango waukazi unabwanthama mwa mikango, unalera ana ake pakati pa misona.

3 Ndipo unalera mmodzi wa ana ake, iye nasanduka msona, unaphunzira kugwira nyama, unalusira anthu.

4 Mitundu ya anthu idamva mbiri yake, unagwidwa m’mbuna mwao; ndipo anadza nao ndi zokowera kudziko la Ejipito.

5 Pakuona tsono waukaziwo, kuti unalindirira, ndi kuti chiyembekezo chake chidatha, unatenga wina wa ana ake, numsandutsa msona.

6 Ndipo unayendayenda pakati pa mikango, nukhala msona, nuphunzira kugwira nyama, nulusira anthu.

7 Ndipo unadziwa amasiye ao, nupasula mizinda yao, ndipo dziko ndi kudzala kwake linasanduka labwinja, chifukwa cha phokoso la kubangula kwake.

8 Pamenepo mitundu ya anthu inadzipereka kuukola kuchokera kumaiko a kumbali zonse, niuphimba ndi ukonde wao, nugwidwa uwu m’mbuna mwao.

9 Nauika m’chitatanga ndi zokowera, nadza nao kwa mfumu ya ku Babiloni; anaulonga m’malinga, kuti mau ake asamvekenso pa mapiri a Israele.

10 Mai wako ananga mpesa wookedwa kumadzi; muja anakhala mumtendere unabala zipatso, wodzala ndi nthambi, chifukwa cha madzi ambiri.

11 Ndipo unali nazo ndodo zolimba zikhale ndodo zachifumu, za ochita ufumu, ndi msinkhu wao unakula kufikira kumitambo, ndipo zinaoneka m’kusomphoka kwao pakati pa nthambi zake zambiri.

12 Koma unazulidwa mwaukali, unaponyedwa pansi ndi mphepo ya kum’mawa, inaumitsa zipatso zake, ndodo zake zolimba zinathyoka ndi kuuma, moto unazitha.

13 Ndipo tsopano waokedwa m’chipululu m’dziko louma ndi la ludzu.

14 Unatulukanso moto kundodo za kunthambi zake, unatha zipatso zake; m’mwemo ulibe ndodo yolimba ikhale ndodo yachifumu ya kuchita ufumu. Iyi ndi nyimbo idzakhala nyimbo ya maliro.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EZK/19-13f826a7a8eed27f6f6df022ee53cead.mp3?version_id=1068—