Ukulu wa Mordekai
1 Ndipo mfumu Ahasuwero inasonkhetsa dziko, ndi zisumbu za ku nyanja.
2 Ndi zochita zonse za mphamvu yake, ndi nyonga zake, ndi mafotokozedwe a ukulu wa Mordekai, umene mfumu inamkulitsa nao, sizinalembedwe kodi m’buku la machitidwe a mafumu a Mediya ndi Persiya?
3 Pakuti Mordekai Myuda anatsatana naye mfumu Ahasuwero, nakhala wamkulu mwa Ayuda, navomerezeka mwa unyinji wa abale ake wakufunira a mtundu wake zokoma, ndi wakunena za mtendere kwa mbeu yake yonse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EST/10-c234db11718620573d237f989aa9d663.mp3?version_id=1068—