Categories
EKSODO

EKSODO 20

Malamulo khumi a Mulungu

1 Ndipo Mulungu ananena mau onse amenewa, nati,

2 Ine ndine Yehova Mulungu wako, amene ndinatulutsa iwe ku dziko la Ejipito, kunyumba ya ukapolo.

3 Usakhale nayo milungu ina koma Ine ndekha.

4 Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena chifaniziro chilichonse cha zinthu za m’thambo la kumwamba, kapena za m’dziko lapansi, kapena za m’madzi a pansi padziko.

5 Usazipembedzere izo, usazitumikire izo; chifukwa Ine Yehova Mulungu wako ndili Mulungu wansanje, wakulanga ana chifukwa cha atate ao, kufikira mbadwo wachitatu ndi wachinai wa iwo amene akudana ndi Ine;

6 ndi kuwachitira chifundo anthu zikwizikwi a iwo amene akondana ndi Ine, nasunga malamulo anga.

7 Usatchule dzina la Yehova Mulungu wako pachabe; chifukwa Yehova sadzamuyesa iye wosachimwa, amene atchula pachabe dzina lakelo.

8 Udzikumbukira tsiku laSabata, likhale lopatulika.

9 Masiku asanu ndi limodzi uzigwira, ndi kumaliza ntchito zako zonse;

10 koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndilo Sabata la Yehova Mulungu wako; usagwire ntchito iliyonse, kapena iwe wekha, kapena mwana wako wamwamuna, kapena mwana wako wamkazi, kapena wantchito wako wamwamuna, kapena wantchito wako wamkazi, kapena nyama zako, kapena mlendo amene ali m’mudzi mwako;

11 chifukwa m’masiku asanu ndi limodzi Yehova adalenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi nyanja ndi zinthu zonse zili m’menemo, napumula tsiku lachisanu ndi chiwiri; chifukwa chake Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika.

12 Uzilemekeza atate wako ndi amai ako; kuti achuluke masiku ako m’dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.

13 Usaphe.

14 Usachite chigololo.

15 Usabe.

16 Usamnamizire mnzako.

17 Usasirire nyumba yake ya mnzako, usasirire mkazi wake wa mnzako, kapena wantchito wake wa mwamuna, kapena wantchito wake wamkazi, kapena ng’ombe yake, kapena bulu wake, kapena kanthu kalikonse ka mnzako.

18 Ndipo anthu onse anaona mabingu ndi zimphezi, ndi liu la lipenga ndi phiri lilikufuka; ndipo pamene anthu anaziona, ananjenjemera, naima patali.

19 Ndipo anati kwa Mose, Mulankhule nafe ndinu, ndipo tidzamva; koma asalankhule nafe Mulungu, kuti tingafe.

20 Ndipo Mose anati kwa anthu, Musaope; pakuti Mulungu wadza kukuyesani ndi kuti kumuopa Iye kukhale pamaso panu, kuti musachimwe

21 Ndipo anthu anaima patali, koma Mose anayandikiza ku mdima waukulu kuli Mulungu.

Za mafano ndi guwa la nsembe

22 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Uzitero ndi ana a Israele, kuti, Mwapenya nokha kuti ndalankhula nanu, kuchokera kumwamba.

23 Musapange milungu yasilivaikhale pamodzi ndi Ine; musadzipangire milungu yagolide.

24 Undiumbire guwa la nsembe ladothi, nundiphere pomwepo nsembe zako zopsereza, ndi nsembe zako zamtendere, nkhosa zako ndi ng’ombe zako; paliponse ndikumbukiritsa anthu dzina langa ndidzakudzera ndi kukudalitsa.

25 Ndipo ukandimangira guwa la nsembe lamiyala, usalimanga ndi miyala yosema; ukakwezapo chosemera chako, waliipsa.

26 Kapena usakwere ndi makwerero ku guwa langa la nsembe, kuti angaoneke maliseche ako pamenepo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/20-5bc76c8798dfd835401df4b93ae30dc7.mp3?version_id=1068—

Categories
EKSODO

EKSODO 21

Lamulo la pa kapolo, ndi la pa wakupha mnzake

1 Ndipo awa ndiwo maweruzo amene uziika pamaso pao.

2 Ukagula mnyamata Muhebri, azigwira ntchito zaka zisanu ndi chimodzi; koma chachisanu ndi chiwiri azituluka waufulu chabe.

3 Akalowa ali yekha azituluka ali yekha; akakhala ndi mkazi, mkazi wake azituluka naye.

4 Akampatsa mkazi mbuye wake, ndipo akambalira ana aamuna ndi aakazi, mkaziyo ndi ana ake azikhala a mbuye wake, ndipo azituluka ali yekha.

5 Koma mnyamatayo akanenetsa, Ndikonda mbuye wanga, mkazi wanga, ndi ana anga; sindituluka waufulu;

6 pamenepo mbuye wake azifika naye kwa oweruza, nafike naye kukhomo, kapena kumphuthu, ndipo mbuye wake am’boole khutu lake ndi lisungulo; ndipo iye azimgwirira ntchito masiku onse.

7 Ndipo munthu akagulitsa mwana wake wamkazi akhale mdzakazi, iyeyu asatuluke monga amatuluka anyamata.

8 Akapanda kumkonda mbuye wake, amene anamtoma mwini yekha, azilola kuti amuombole; alibe mphamvu yakumgulitsa kwa anthu achilendo, popeza wachita naye monyenga.

9 Koma ngati amtomera mwana wake wamwamuna, amchitire monga kuyenera ana aakazi.

10 Akamtengera mkazi wina, asachepetse chakudya chake, zovala zake, ndi za ukwati zakezake.

11 Ndipo akapanda kumchitira izi zitatu, azituluka chabe, osaperekapo ndalama.

12 Iye amene akantha munthu kotero kuti wafa, aphedwe ndithu.

13 Koma akapanda kumlalira, koma Mulungu akalola akomane ndi mnzake, ndidzakuikirani pothawirapo iye.

14 Koma munthu akachita dala pa mnzake, kumupha monyenga; uzimchotsa ku guwa langa la nsembe, kuti afe.

15 Munthu wakukantha atate wake, kapena amai wake, aphedwe ndithu.

16 Iye wakuba munthu, angakhale wamgulitsa, kapena akampeza m’dzanja lake, aphedwe ndithu.

Malamulo a pa wotemberera ombala ndi opweteka anzao

17 Munthu wakutemberera atate wake, kapena amai wake, aphedwe ndithu.

18 Akalimbana amuna, ndipo wina akakantha mnzake ndi mwala, kapena ndi nkhonya, wosafa iye, koma wakhulungira pakama;

19 akaukanso, nakayendayenda pabwalo ndi ndodo yake, womkanthayo azikhala womasuka; pakutsotsa pake pokha azimbwezera, namchizitse konse.

20 Munthu akakantha mnyamata wake, kapena mdzakazi wake, ndi ndodo, ndipo akafa padzanja pake; ameneyo alangidwe ndithu.

21 Koma akakhala wosafa tsiku limodzi kapena awiri, asalangike, pakuti ndiye ndalama ya mbuye wake.

22 Akayambana amuna, nakakantha mkazi ali ndi pakati, kotero kuti abala, koma alibe kuphwetekwa; alipe ndithu, monga momwe amtchulira mwamuna wa mkaziyo; apereke monga anena oweruza.

23 Koma ngati kupweteka kukalipo, uzipereka moyo kulipa moyo,

24 diso kulipa diso, dzino kulipa dzino, dzanja kulipa dzanja, phazi kulipa phazi,

25 kutentha kulipa kutentha, bala kulipa bala, mkwapulo kulipa mkwapulo.

26 Munthu akampanda mnyamata wake, kapena mdzakazi wake, padiso, nalithudzula, azimlola amuke waufulu chifukwa cha diso lake.

27 Ndipo akagulula dzino la mnyamata wake, kapena dzino la mdzakazi wake, azimlola amuke waufulu chifukwa cha dzino lake.

28 Ng’ombe ikatunga mwamuna kapena mkazi, nafa, aiponyetu miyala ng’ombeyo, osadya nyama yake; koma mwini ng’ombeyo azimasuka.

29 Koma ngati ng’ombe ikatunga masiku adapitawo, ndipo anamchenjeza mwiniyo, koma osaisunga iye, ndipo ikapha mwamuna kapena mkazi, aiponye miyala ng’ombeyo, ndi mwini wakeyo amuphenso.

30 Akamuikira dipo, azipereka chiombolo cha moyo wake monga mwa zonse adamuikira.

31 Ingakhale yatunga mwana wamwamuna kapena wamkazi, aichitire monga mwa chiweruzo ichi.

32 Ng’ombeyo ikatunga mnyamata kapena mdzakazi, azipatsa mbuye wake ndalama za masekeli asilivamakumi atatu, ndipo ng’ombeyo aiponye miyala.

Malamulo a pa chuma

33 Munthu akafukula dzenje, kapena akakumba dzenje, osalivundikira, ndipo ikagwamo ng’ombe kapena bulu,

34 mwini dzenje azilipa; azilipa ndalama kwa mwini nyamayo, koma yakufayo ndi yake.

35 Ng’ombe ya mwini ikapweteka ng’ombe ya mnzake, nifa, azigulitsa ng’ombe yamoyoyo, nagawe ndalama zake; naigawe, ndi yakufa yomweyo.

36 Kapena kudadziwika kuti ng’ombe ikatunga masiku adapitawo, koma osaisunga mwiniyo, azilipa ndithu, ng’ombe kulipa ng’ombe, koma yakufayo ndi yake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/21-82bf9b8d9c450e7d042ba38bab76141b.mp3?version_id=1068—

Categories
EKSODO

EKSODO 22

1 Munthu akaba ng’ombe, kapena nkhosa, nakaipha kapena kuigulitsa, azilipa ng’ombe zisanu pa ng’ombeyo, ndi nkhosa zinai pa nkhosayo.

2 Akampeza wakuba alimkuboola, nakamkantha kotero kuti wafa, palibe chamwazi.

3 Litamtulukira dzuwa, pali chamwazi; wakubayo azilipa ndithu; ngati alibe kanthu, amgulitse pa umbala wake.

4 Akachipeza chakubacho chili m’dzanja lake chamoyo, ngakhale ng’ombe, kapena bulu, kapena nkhosa, alipe mowirikiza.

5 Munthu akadyetsa choweta pabusa kapena pamunda wampesa, atamasula choweta chake, ndipo chitadya podyetsa pa mwini wake; alipe podyetsa pake poposa, ndi munda wa mphesa wake woposa.

6 Ukayaka moto, nukalandira kuminga, kotero kuti unyeketsa mulu wa tirigu, kapena tirigu wosasenga, kapena munda; woyatsa motoyo alipe ndithu.

7 Munthu akaikiza ndalama kapena chuma kwa mnansi wake, ndipo zibedwa m’nyumba ya munthuyo; akapeza mbala, ilipe chowirikiza.

8 Akapanda kumpeza mbalayo, abwere naye mwini nyumbayo kwa oweruza, kumuyesa ngati anaika dzanja lake pa chuma cha mnansi wake.

9 Mlandu uliwonse wa cholakwa, kunena za ng’ombe, za bulu, za nkhosa, za chovala, za kanthu kalikonse kotayika, munthu anenako kali kake; mlandu wa onse awiri ufike kwa oweruza; iye amene oweruza amtsutsa alipe chowirikiza kwa mnansi wake.

10 Munthu akaikiza bulu, kapena ng’ombe, kapena nkhosa, kapena choweta china kwa mnansi wake, ndipo chikafa, kapena chiphwetekwa, kapena wina achipirikitsa osachiona munthu;

11 lumbiro la Yehova likhale pakati pa iwo awiri, kuti sanatulutse dzanja lake pa chuma cha mnansi wake; ndipo mwiniyo azivomereza, ndipo asalipe.

12 Koma ngati chidabedwa kwaoko ndithu, alipe kwa mwiniyo.

13 Ngati chajiwa ndithu, abwere nacho chikhale mboni; asalipe pa chojiwacho.

14 Munthu akabwereka chinthu kwa mnansi wake, ndipo chiphwetekwa, kapena chifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu.

15 Akakhalapo mwiniyo, asalipe; ngati chagwirira ntchito yakulipira, chadzera kulipira kwake.

Malamulo osiyanasiyana a pakati pa anthu

16 Munthu akanyenga namwali wosapalidwa ubwenzi, nakagona naye, alipetu kuti akhale mkazi wake.

17 Atate wake akakana konse kumpatsa iye, alipe ndalama monga mwa cholipa cha anamwali.

18 Wanyanga usamlola akhale ndi moyo.

19 Aliyense agona ndi choweta aphedwe ndithu.

20 Wakuphera nsembe mulungu wina, wosati Yehova yekha, aonongeke konse.

21 Ndipo usasautsa mlendo kapena kumpsinja; pakuti munali alendo m’dziko la Ejipito.

22 Musazunza mkazi wamasiye, kapena mwana wamasiye aliyense.

23 Ukawazunza ndi kakuti konse, nakandilirira pang’ono ponse iwowa, ndidzamvadi kulira kwao;

24 ndi mkwiyo wanga udzayaka, ndipo ndidzapha inu ndi lupanga; ndipo akazi anu adzakhala amasiye, ndi ana anu omwe.

25 Ukakongoletsa ndalama anthu anga osauka okhala nanu, usamkhalira ngati wangongole; usamuwerengera phindu.

26 Ukati ulandire chikole kaya chovala cha mnansi wako, koma polowa dzuwa uchibwezere kwa iye;

27 popeza chofunda chake ndi ichi chokha, ndicho chovala cha pathupi pake; azifundira chiyani pogona? Ndipo kudzakhala kuti akandifuulira Ine, ndidzamva; pakuti Ine ndine wachisomo.

28 Usapeputsa oweruza, kapena kutemberera mkulu wa anthu a mtundu wako.

29 Usachedwa kuperekako zipatso zako zochuluka, ndi zothira zako. Woyamba wa ana ako aamuna undipatse Ine.

30 Uzitero nazo ng’ombe zako, ndi nkhosa zako; masiku asanu ndi atatu akhale ndi amai wake; tsiku lachisanu ndi chitatu uzimpereka kwa Ine.

31 Ndipo muzindikhalira Ine anthu opatulika; chifukwa chake musamadya nyama yojiwa kuthengo; itayireni agalu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/22-3fc304c4662b6e5062745e37f8daf452.mp3?version_id=1068—

Categories
EKSODO

EKSODO 23

Za mabodza ndi zonyenga

1 Usatola mbiri yopanda pake; usathandizana naye woipa ndi kukhala mboni yochititsa chiwawa.

2 Usatsata unyinji wa anthu kuchita choipa; kapena usachita umboni kumlandu, ndi kupatukira kutsata unyinji ndi kukhotetsa mlandu;

3 kapena usakometsera munthu wosauka pa mlandu wake.

4 Ukakomana ndi ng’ombe kapena bulu wa mdani wako zilinkusokera, uzimbwezera izo ndithu.

5 Ukaona bulu wa munthu wakudana nawe alikugona pansi ndi katundu wake, ndipo ukadaleka kuthandiza, koma uzimthandiza ndithu.

6 Usakhotetsa mlandu wa mnzako waumphawi.

7 Uzikhala kutali ndi mlandu wonama; ndipo usapha munthu wosachimwa ndi wolungama; pakuti sindidzayesa wolungama munthu woipa.

8 Usalandira chokometsera mlandu; pakuti chokometsera mlandu chidetsa maso a openya, ndipo chisanduliza mlandu wa olungama.

9 Usampsinja mlendo; pakuti mudziwa mtima wa mlendo popeza munali alendo m’dziko la Ejipito.

Za nthawi zopumula

10 Ndipo uzibzala m’munda mwako zaka zisanu ndi chimodzi, ndi kututa zipatso zako;

11 koma chaka chachisanu ndi chiwiri uuleke, ugone; kuti aumphawi a anthu a mtundu wako adyemo, ndipo zotsalira nyama zakuthengo zizidye; momwemo uzichita ndi munda wako wampesa, ndi munda wako waazitona.

12 Uzichita ntchito yako masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri uzipumula; kuti ng’ombe yako ndi bulu wako zipumule, ndi kuti mwana wa mdzakazi wako ndi mlendo atsitsimuke.

13 Ndipo samalirani zonse ndanena ndi inu; nimusatchule dzina la milungu ina; lisamveke pakamwa pako.

Za madyerero atatu m’chaka

14 Muzindichitira Ine madyerero katatu m’chaka.

15 Uzisungachikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa; masiku asanu ndi awiri uzidya mkate wopanda chotupitsa, monga ndinakuuza, nyengo yoikika, mwezi wa Abibu, pakuti m’menemo unatuluka mu Ejipito; koma asaoneke munthu pamaso panga opanda kanthu;

16 ndichikondwerero cha Masika, zipatso zoyamba za ntchito zako, zimene udazibzala m’munda; ndi chikondwerero cha Kututa, pakutha chaka, pamene ututa ntchito zako za m’munda.

17 Katatu m’chaka amuna onse azioneka pamaso pa Ambuye Yehova.

18 Usapereka mwazi wa nsembe yanga pamodzi ndi mkate wa chotupitsa; ndi mafuta a madyerero anga asagonamo kufikira m’mawa.

19 Uzibwera nazo zoyambayamba za m’munda mwako kunyumba ya Yehova Mulungu wako. Usaphike mwanawambuzi mu mkaka wa make.

Mulungu alonjezana nao za Kanani

20 Taona, ndituma mthenga akutsogolere, kukusunga panjira, ndi kukufikitsa pamaso pomwe ndakonzeratu.

21 Musamalire iye, ndi kumvera mau ake; musamuwawitsa mtima, pakuti sadzakhululukira zolakwa zanu; popeza dzina langa lili m’mtima mwake.

22 Pakuti ukamveratu mau ake, ndi kuchita zonse ndizilankhula, ndidzakhala mdani wa adani ako, ndipo ndidzasautsa akusautsa iwe.

23 Pakuti mthenga wanga adzakutsogolera, nadzakufikitsa kwa Aamori, ndi Ahiti, ndi Aperizi, ndi Akanani, Ahivi, ndi Ayebusi; ndipo ndidzawaononga.

24 Usagwadira milungu yao, kapena kuwatumikira, kapena kuchita monga mwa ntchito zao; koma uwapasule konse, ndi kugamulatu zoimiritsa zao.

25 Ndipo muzitumikira Yehova Mulungu wanu, potero adzadalitsa chakudya chako, ndi madzi ako; ndipo ndidzachotsa nthenda pakati pa iwe.

26 M’dziko mwanu simudzakhala wakutaya mwana, kapena wosabala; ndidzakwaniritsa kuwerenga kwa masiku ako.

27 Ndidzatumiza kuopsa kwanga kukutsogolere, ndipo ndidzapirikitsa anthu onse amene udzafika kwao, ndipo ndidzachita kuti adani ako onse adzakuonetsa m’mbuyo mwao.

28 Ndipo ndidzatumiza mavu akutsogolere amene adzaingitsa Ahivi, Akanani, ndi Ahiti, pamaso pako.

29 Sindidzawaingitsa pamaso pako chaka chimodzi; kuti dziko lingakhale bwinja, ndi zilombo zakuthengo zingakuchulukire.

30 Ndidzawaingitsa pang’onopang’ono pamaso pako, kufikira utachuluka, ndi kulandira dziko cholowa chako.

31 Ndipo ndidzalemba malire ako kuyambira ku Nyanja Yofiira, kufikira ku nyanja ya Afilisti, ndi kuyambira kuchipululu kufikira ku Nyanja; popeza ndidzapereka okhala m’dzikolo m’dzanja lako, ndipo uziwaingitsa pamaso pako.

32 Usapangana nao, kapena ndi milungu yao.

33 Asakhale m’dziko lako iwowa, kuti angakulakwitse pa Ine; pakuti ukatumikira milungu yao, kudzakukhalira msampha ndithu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/23-9a4a96869e9ec6834a0af6278544f917.mp3?version_id=1068—

Categories
EKSODO

EKSODO 24

Mose ndi akulu akwera m’phiri

1 Ndipo Iye ananena ndi Mose, Ukwere kudza kwa Yehova, iwe ndi Aroni, Nadabu ndi Abihu, ndi akulu a Israele makumi asanu ndi awiri; ndipo mugwadire pakudza kutali;

2 ndipo Mose yekha ayandikire kwa Yehova; koma asayandikire iwowa; ndi anthunso asakwere naye.

3 Ndipo Mose anadza nafotokozera anthu mau onse a Yehova, ndi maweruzo onse; ndipo anthu onse anavomera pamodzi, nati, Mau onse walankhula Yehova tidzachita.

4 Ndipo Mose analembera mau onse a Yehova, nalawira kuuka mamawa, namanga guwa la nsembe patsinde paphiri, ndi zoimiritsa khumi ndi ziwiri, kwa mafuko khumi ndi awiri a Israele.

5 Ndipo anatuma ana a Israele a misinkhu ya anyamata, ndiwo anapereka nsembe zopsereza, naphera Yehova nsembe zamtendere, za ng’ombe.

6 Ndipo Mose anagawa mwaziwo, nathira wina m’zotengera, nawaza wina paguwa la nsembe

7 Ndipo anatenga buku laChipangano, nawerenga m’makutu a anthu; ndipo iwo anati, Zonse zimene Yehova walankhula tidzachita, ndi kumvera.

8 Ndipo Mose anatenga mwaziwo, nawaza pa anthu, nati Taonani mwazi wa chipangano, chimene Yehova anachita nanu, kunena za mau awa onse.

9 Ndipo Mose ndi Aroni, Nadabu ndi Abihu, ndi akulu a Israele makumi asanu ndi awiri anakwerako;

10 ndipo anapenya Mulungu wa Israele; ndipo pansi pa mapazi ake panali ngati mayalidwe oyera a miyala yasafiro, ndi ngati thupi la thambo loti mbee.

11 Koma sanatulutse dzanja lake pa akulu a ena a Israele; ndipo anapenya Mulungu, nadya, namwa.

12 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Ukwere kudza kwa Ine m’phiri muno, nukhale pompano; ndipo ndidzakupatsa magome amiyala, ndi chilamulo ndi malamulo ndawalembera kuti uwalangize.

13 Ndipo anauka Mose, ndi Yoswa mtumiki wake; ndipo Mose anakwera m’phiri la Mulungu.

14 Ndipo anati kwa akulu, Tilindeni kuno kufikira tidzabwera kwa inu; ndipo taonani, Aroni ndi Huri ali nanu; munthu akakhala ndi mlandu abwere kwa iwowa.

15 Ndipo Mose anakwera m’phirimo, ndi mtambo unaphimba phirilo.

16 Ndipo ulemerero wa Yehova unakhalabe paphiri la Sinai, ndi mtambo unaliphimba masiku asanu ndi limodzi; ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri Iye ali m’kati mwa mtambo anaitana Mose.

17 Ndipo maonekedwe a ulemerero wa Yehova anali ngati moto wonyeketsa pamwamba paphiri, pamaso pa ana a Israele.

18 Ndipo Mose analowa m’kati mwa mtambo, nakwera m’phirimo; ndipo Mose anakhala m’phiri masiku makumi anai usana ndi usiku.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/24-ce154869f3341483f43b4722f4931bf9.mp3?version_id=1068—

Categories
EKSODO

EKSODO 25

Zopereka zaufulu zakumanga Malo Opatulika

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2 Lankhula ndi ana a Israele, kuti anditengere chopereka; ulandire chopereka changa kwa munthu aliyense mtima wake umfunitsa mwini.

3 Ndipo choperekacho uchilandire kwa iwo ndi ichi: golide, ndisiliva, ndi mkuwa,

4 ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;

5 ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonyika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wakasiya;

6 mafuta akuunikira, zonunkhira za mafuta odzoza, ndi za chofukiza cha fungo lokoma;

7 miyala yaberulo, ndi miyala yoika paefodi, ndi pachapachifuwa.

8 Ndipo andimangire malo opatulika; kuti ndikhale pakati pao.

9 Monga mwa zonse Ine ndilikuonetsa iwe, chifaniziro cha chihema, ndi chifaniziro cha zipangizo zake zonse, momwemo uchimange.

Za likasa, chotetezerapo, ndi akerubi

10 Ndipo azipanga likasa la mtengo wakasiya: utali wake mikono iwiri ndi hafu, kupingasa kwake mkono ndi hafu, msinkhu wake mkono ndi hafu.

11 Ndipo ulikute ndi golide woona, ulikute m’kati ndi kubwalo, nulipangire mkombero wagolide pozungulira pake.

12 Ndipo uliyengere mphete zinai zagolide, ndi kuziika kumiyendo yake inai; mphete ziwiri pa mbali yake ina, ndi mphete ziwiri pa ina.

13 Ndipo uzipanga mphiko za mtengo wakasiya, ndi kuzikuta ndi golide.

14 Nupise mphiko m’mphetezo pa mbali zake za likasa, zakunyamulira nazo likasalo.

15 Mphiko zikhale m’zimphete za likasa; asazisolole.

16 Ndipo uziika m’likasamo mboni imene ndidzakupatsa.

17 Ndipo uzipanga chotetezerapo cha golide woona; utali wake mikono iwiri ndi hafu, ndi kupingasa kwake mkono ndi hafu.

18 Uzipangansoakerubiawiri agolide; uwasule mapangidwe ake, pa mathungo ake awiri a chotetezerapo.

19 Nupange kerubi mmodzi ku thungo lino, ndi kerubi wina ku thungo lina; upange akerubi ochokera kuchotetezerapo, pa mathungo ake awiri.

20 Ndipo akerubi afunyululire mapiko ao m’mwamba, ndi kuphimba chotetezerapo ndi mapiko ao, ndi nkhope zao zipenyane; nkhope za akerubi zipenye kuchotetezerapo.

21 Ndipo uziika chotetezerapo pamwamba pa likasa, ndi kuikamo mboni ndidzakupatsayo m’likasamo.

22 Ndipo pomwepo ndidzakomana ndi iwe, ndi kulankhula ndi iwe, ndili pamwamba pa chotetezerapo, pakati pa akerubi awiriwo okhala pa likasa la mboni, zonse zimene ndidzakuuza za ana a Israele.

Za gome la mkate woonekera

23 Ndipo uzipanga gome la mtengo wakasiya; utali wake mikono iwiri, ndi kupingasa kwake mkono umodzi, ndi msinkhu wake mkono ndi hafu.

24 Ndipo ulikute ndi golide woona ndi kulipangira mkombero wagolide pozungulira pake.

25 Nulipangire mitanda pozungulirapo yoyesa chikhato m’kupingasa kwake, ndi pamitanda pake pozungulira upangirepo mkombero wagolide.

26 Nulipangire mphete zinai zagolide, ndi kuika mphetezo pangodya zinai zokhala pa miyendo yake inai.

27 Mphetezo zikhale pafupi pa mitanda, zikhale zopisamo mphiko za kunyamulira nazo gome.

28 Ndipo uzipanga mphiko za mtengo wakasiya, ndi kuzikuta ndi golide, kuti anyamulire nazo gome.

29 Ndipo uzipanga mbale zake, ndi zipande zake, ndi mitsuko yake, ndi zikho zake zakuthira nazo; uzipanga za golide woona.

30 Ndipo uziika mkate woonekera pa gomelo pamaso panga nthawi zonse.

Za choikaponyali

31 Ndipo uzipanga choikaponyali cha golide woona; choikapocho chisulidwe mapangidwe ake, tsinde lake ndi thupi lake; zikho zake, mitu yake, ndi maluwa ake zikhale zochokera m’mwemo;

32 ndipo m’mbali zake mutuluke mphanda zisanu ndi imodzi; mphanda zitatu za choikaponyalicho zituluke m’mbali yake ina, ndi mphanda zitatu za choikaponyalicho zituluke m’mbali inzake.

33 Ku mphanda ina kukhale zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi duwa; ndi ku mphanda inzake zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi duwa; zitere mphanda zisanu ndi imodzi zotuluka m’choikaponyalicho.

34 Ndipo pa choikaponyali chomwe pakhale zikho zinai zopangika ngati katungurume, mitu yake ndi maluwa ake;

35 pakhale mutu pansi pa mphanda ziwiri zotuluka m’mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri zotuluka m’mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri zotuluka m’mwemo; itere ku mphanda zisanu ndi imodzi zotuluka m’choikaponyalicho.

36 Mitu yao ndi mphanda zao zikhale zotuluka m’mwemo; chonsechi chikhale chosulika chimodzi cha golide woona.

37 Ndipo uzipanga nyali zake, zisanu ndi ziwiri; ndipo ayatse nyali zake, ziwale pandunji pake.

38 Ndipo mbano zake, ndi zoolera zake, zikhale za golide woona.

39 Achipange ichi ndi zipangizo izi zonse za talente wa golide woona.

40 Ndipo uyang’anire uzipanga monga mwachifaniziro chao, chimene anakuonetsa m’phirimo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/25-3eb74f44fc77334dd16db707f0e1263c.mp3?version_id=1068—

Categories
EKSODO

EKSODO 26

Chihema ndi nsalu zophimba zake

1 Ndipo uzipanga chihema ndi nsalu zophimba khumi, za bafuta wa thonje losansitsa, ndi thonje lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira; uombemoakerubi, ntchito ya mmisiri.

2 Utali wake wa nsalu yophimba imodzi ndiwo mikono makumi awiri kudza isanu ndi itatu, ndi kupingasa kwa nsalu imodzi ndiko mikono inai; nsalu zonse zikhale za muyeso umodzi.

3 Nsalu zisanu zilumikizane ina ndi inzake; ndi nsalu zisanu zina zilumikizane ina ndi inzake.

4 Ndipo uziika magango a nsalu ya madzi m’mphepete mwake mwa nsalu imodzi, ku mkawo wa chilumikizano; nuchite momwemo m’mphepete mwake mwa nsalu ya kuthungo ya chilumikizano china.

5 Uziika magango makumi asanu pansalu yochingira imodzi, nuikenso magango makumi asanu m’mphepete mwake mwa nsalu ya chilumikizano china; ndipo magango akomanizane lina ndi linzake.

6 Uzipanganso zokowera makumi asanu zagolide, ndi kumanga nsaluzo pamodzi ndi zokowerazo; kuti chihema chikhale chimodzi.

7 Ndipo uziomba nsalu zophimba za ubweya wa mbuzi zikhale chophimba pamwamba pa chihema; uziomba nsalu khumi ndi imodzi.

8 Utali wake wa nsalu imodzi ndiwo mikono makumi atatu, ndi kupingasa kwake kwa nsalu imodzi ndiko mikono inai; nsalu khumi ndi imodzi zikhale za muyeso womwewo.

9 Nuzisoka pamodzi nsalu zisanu pazokha, ndi nsalu zisanu ndi imodzi pazokha, nupinde nsalu yachisanu ndi chimodziyo pa khomo la hema.

10 Ndipo uziika magango makumi asanu m’mphepete mwa nsalu imodzi, ya kuthungo ya chilumikizano, ndi magango makumi asanu m’mphepete mwa nsalu ya kuthungo ya chilumikizano china.

11 Ndipo uzipanga zokowera makumi asanu zamkuwa, ndi kukowetsa zokowerazo m’magangomo, ndi kumanga pamodzi hemalo likhale limodzi.

12 Ndipo chotsalacho pansalu yophimbayo, hafu yake ya nsalu yotsalirayo, itchinge pambuyo pake pa chihemacho.

13 Ndi mkono wa pa mbali ino, ndi mkono wa pa mbali inzake, wakutsalira mu utali wake wa nsalu zophimbazo, itchinge pambali zake za chihemacho, mbali ino ndi mbali ina, kumphimba.

14 Ndipo uzipangira hema chophimba cha zikopa za nkhosa zamphongo zonyika zofiira, ndi chophimba za zikopa za akatumbu pamwamba pake.

Za matabwa oimirika a chihema

15 Ndipo uzipangira chihema matabwa oimirika, a mtengo wakasiya.

16 Utali wake wa thabwa limodzi ndiwo mikono khumi, ndi kupingasa kwake kwa thabwali mkono ndi hafu.

17 Pa thabwa limodzi pakhale mitsukwa iwiri, yomangika pamodzi; uzitero pa matabwa onse a chihema.

18 Ndipo uzipanga matabwa a chihema, matabwa makumi awiri ku mbali ya kumwera, kumwera.

19 Nuzipanga makamwa makumi anai asilivapansi pa matabwa makumi awiri; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi kwa mitsukwa yake iwiri, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina kwa mitsukwa yake iwiri;

20 ndi pa mbali yake ina ya chihema, mbali ya kumpoto, pakhale matabwa makumi awiri; ndi makamwa asiliva makumi anai;

21 makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina.

22 Ndipo uzipanga matabwa asanu ndi limodzi kwa mbali ya chihema cha kumbuyo.

23 Nupange matabwa awiri angodya za chihema cha kumbuyo.

24 Ndipo akhale ophatikizika pamodzi patsinde, nakhalenso ophatikizika pamodzi kumutu kwake ndi mphete imodzi; azitero onse awiri; azikhala angodya ziwiri.

25 Ndipo pakhale matabwa asanu ndi atatu, ndi makamwa ao asiliva, ndiwo makamwa khumi mphambu asanu ndi limodzi; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina.

26 Ndipo uzipanga mitanda ya mtengo wakasiya; isanu ya matabwa a pa mbali ina ya chihema,

27 ndi mitanda isanu ya matabwa a pa mbali ina ya chihema, ndi mitanda isanu ya matabwa a pa mbali ya chihema cha kumbuyo kumadzulo.

28 Ndi mtanda wa pakati pa matabwa ufikire kuthungo.

29 Ndipo uzikuta matabwa ndi golide, ndi kupanga mphete zao zagolide zopisamo mitandayo; uzikutanso mitandayo ndi golide.

30 Ndipo uutse chihema monga mwa makhalidwe ake amene anakusonyeza m’phiri.

Za nsalu yosiyanitsa ya pakhomo

31 Ndipo uziomba nsalu yotchinga ya thonje lamadzi, ndi lofiirira ndi lofiira, ndi la bafuta wa thonje losansitsa, aiombe ndi akerubi ntchito ya mmisiri;

32 ndipo uitchinge pa mizati inai ya mitengo wakasiya, zokuta ndi golide; zokowera zao zikhale zagolide, ndi makamwa anai asiliva.

33 Ndipo uzitchinga nsalu yotchinga pa zokowerazo, nulowetse likasa la mboni kukati kwa nsalu yotchinga; ndipo nsalu yotchingayo idzakugawirani pakati pa malo opatulika ndi malo opatulika kwambiri.

34 Ndipo uziika chotetezerapo pa likasa la mboni, m’malo opatulika kwambiri.

35 Nuziika gomelo kunja kwa nsalu yotchinga, ndi choikaponyali pandunji pa gome, pa mbali ya kumwera ya chihema; koma uike gomelo pa mbali ya kumpoto.

36 Ndipo uziomba nsalu yotsekera pa khomo la hema, ya lakuda, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ntchito ya wopikula.

37 Ndipo uzipangira nsalu yotsekerayo nsanamira zisanu za mtengo wakasiya, ndi kuzikuta ndi golide; zokowera zao zikhale zagolide; nuziyengera makamwa asanu amkuwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/26-8341ceb2770dc65361d78f2556c37352.mp3?version_id=1068—

Categories
EKSODO

EKSODO 27

Za guwa la nsembe

1 Ndipo upange guwa la nsembe la mtengo wakasiya, utali wake mikono isanu, ndi kupingasa kwake mikono isanu, guwa la nsembelo likhale laphwamphwa, ndi msinkhu wake mikono itatu.

2 Ndipo uzipanga nyanga zake pangodya zake zinai; nyanga zake zikhale zotuluka m’mwemo: nulikute ndi mkuwa.

3 Ndipo uzipanga zotayira zake zakulandira mapulusa ake, ndi zoolera zake, ndi mbale zowazira zake, ndi mitungo yake, ndi zopalira moto zake; zipangizo zake zonse uzipanga zamkuwa.

4 Ndipo ulipangire sefa, malukidwe ake ndi amkuwa; nupange pa malukidwewo ngodya zake zinai mphete zinai zamkuwa.

5 Nuwaike pansi pa khoma lamkati la guwa la nsembelo posungulira, kuti malukidwe alekeze pakati pa guwa la nsembelo.

6 Ndipo upangire guwa la nsembe mphiko, mphiko za mtengo wakasiya, ndi kuzikuta ndi mkuwa.

7 Ndipo apise mphiko m’mphetezo kuti mphikozo zikhale pa mbali ziwiri za guwa la nsembe polinyamula.

8 Ulipange lagweregwere ndi matabwa; monga anakuonetsa m’phirimo; alipange momwemo.

Za bwalo la chihema

9 Upangenso bwalo la chihema; pa mbali yake ya kumwera, kumwera, pakhale nsalu zotchingira za kubwalo za nsalu yabafuta wa thonje losansitsa, utali wake wa pa mbali imodzi mikono zana;

10 ndi nsichi zake makumi awiri, ndi makamwa ao makumi awiri akhale amkuwa; zokowera za nsichi ndi mitanda yake zikhale zasiliva.

11 Momwemonso pa mbali ya ku kumpoto mu utali mwake pakhale nsalu zotchingira za mikono zana limodzi mu utali mwake; ndi nsichi zake makumi awiri, ndi makamwa ao akhale amkuwa; zokowera za nsichizo ndi mitanda yake zikhale zasiliva.

12 Ndipo m’kupingasa kwa bwaloli pa mbali ya kumadzulo mukhale nsalu zotchingira za mikono makumi asanu; nsichi zake zikhale khumi, ndi makamwa ao khumi.

13 Ndipo m’kupingasa kwake kwa bwalo pa mbali ya kum’mawa, kum’mawa, mukhale mikono makumi asanu.

14 Ndi nsalu zotchingira za pa mbali imodzi ya kuchipata zikhale za mikono khumi ndi isanu; nsichi zake zikhale zitatu, ndi makamwa ao atatu.

15 Ndi pa mbali ina pakhale nsalu zotchingira za mikono khumi ndi isanu; nsichi zake zikhale zitatu, ndi makamwa ao atatu.

16 Ndipo pa chipata cha bwalolo pakhale nsalu yotsekera ya mikono makumi awiri, ya lamadzi ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ntchito ya wopikula; nsichi zake zikhale zinai, ndi makamwa ao anai.

17 Nsichi zonse za pabwalo pozungulira zimangike pamodzi ndi mitanda yasiliva; zokowera zao zasiliva, ndi makamwa ao amkuwa.

18 Utali wake wa bwalolo ukhale wa mikono zana limodzi, ndi kupingasa kwake makumi asanu monsemo, ndi msinkhu wake wa mpanda mikono isanu; ukhale wabafuta wa thonje losansitsa; ndi makamwa a nsichizo akhale amkuwa.

19 Zipangizo zonse za chihema, m’machitidwe ake onse, ndi zichiri zake zonse, ndi zichiri zonse za bwalo lake, zikhale zamkuwa.

Za mafuta a nyaliyo

20 Ndipo uuze ana a Israele akutengere mafuta a azitona oyera opera akuunikira, kuti awalitse nyali kosalekeza.

21 Aroni ndi ana ake aikonze m’chihema chokomanako, pamaso pa Yehova, kunja kwa nsalu yotchinga yokhala kumboni, kuyambira madzulo kufikira m’mawa; likhale lemba losatha mwa mibadwo yao, alisunge ana a Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/27-80511f10eef8db2979e3e93473170f77.mp3?version_id=1068—

Categories
EKSODO

EKSODO 28

Za zovala zopatulika

1 Ndipo akuyandikire Aroni mbale wako, ndi ana ake aamuna pamodzi naye, mwa ana a Israele, kuti andichitire Ine ntchito ya nsembe, ndiwo Aroni, Nadabu, ndi Abihu, Eleazara ndi Itamara, ana a Aroni.

2 Ndipo usokere Aroni mbale wako zovala zopatulika, zikhale zaulemerero ndi zokoma.

3 Ndipo ulankhule ndi onse a mtima waluso, amene ndawadzaza ndi mzimu waluso, kuti amsokere Aroni zovala apatulidwe nazo, andichitire Ine ntchito ya nsembe.

4 Ndipo zovala azisoka ndi izi: chapachifuwa ndiefodi, ndi mwinjiro, ndi malaya opikapika, ndi nduwira, ndi mpango; tero apangire Aroni mbale wako ndi ana ake zovala zopatulika, kuti andichitire Ine ntchito ya nsembe.

5 Ndipo atenge golide, ndi lamadzi ndi lofiirira ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

Za Efodi

6 Naombe efodi ndi golide, ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira ndi bafuta wa thonje losansitsa, ntchito ya mmisiri.

7 Akhale nazo zapamapewa ziwiri zomangika ku nsonga zake ziwiri, kuti amangike nazo.

8 Ndipo mpango wa efodi, wokhala pamenepo, kuti ammange nao, ukhale wa chiombedwe chomwecho, ndi woombera kumodzi, wagolide, ndi thonje lamadzi, ndi lofiirira ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

9 Ndipo utenge miyala iwiri yaberulo, nulochepo maina a ana a Israele;

10 maina asanu ndi limodzi pamwala wina, ndi maina asanu ndi limodzi otsala pamwala unzake, mwa kubadwa kwao.

11 Uloche miyala iwiriyo ndi maina a ana a Israele, monga mwa ntchito ya wolocha miyala, monga malembedwe a chosindikizira, uipange igwirike ndi zoikamo zagolide.

12 Ndipo uiike miyala iwiriyo pa zapamapewa za efodi, ikhale miyala ya chikumbutso cha ana a Israele; ndipo Aroni azinyamula maina ao pa mapewa ake awiri, akhale chikumbutso pamaso pa Yehova.

13 Ndipo upange zoikamo za golide;

14 ndi maunyolo awiri a golide woona; uwapote ngati zingwe, ntchito yopota; numange maunyolo opotawo pazoikamo.

Za chapachifuwa

15 Upangenso chapachifuwa cha chiweruzo, ntchito ya mmisiri; uchiombe mwa chiombedwe cha efodi; uchiombe ndi golide, lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

16 Chikhale chaphwamphwa, chopindika, utali wake dzanja limodzi, ndi kupingasa kwake dzanja limodzi.

17 Ndipo uikepo miyala yoikikapo, mizere inai ya miyala; mzere wa odemu, pitida, ndi bareketi, ndiyo ya mzere woyamba;

18 ndi mzere wachiwiri wa nofeki, safiro, ndi yahaloni;

19 ndi mzere wachitatu wa lesemu, sibu, ndi akalama;

20 ndi mzere wachinai wa tarisisi, sohamu, ndi yasefe; zikhale zogwirika ndi golide m’zoikamo zao.

21 Ndi miyalayi ikhale monga mwa maina a ana a Israele, khumi ndi awiri, monga maina ao; monga malochedwe a chosindikizira, yonse ikhale monga maina ao, kwa mafuko khumi ndi awiri.

22 Upangenso maunyolo pa chapachifuwa ngati zingwe, ntchito yopota, ya golide woona.

23 Nupangire pa chapachifuwa mphete ziwiri zagolide, ndi kuzika mphete ziwirizo pansonga zake ziwiri za chapachifuwa.

24 Numange maunyolo awiri opota agolide ku mphete ziwirizo pansonga pake pa chapachifuwa.

25 Koma nsonga zake ziwiri za maunyolo opotawo uzimange ku zoikamo ziwiri, ndi kuziika pa zapamapewa ziwiri za efodi, m’tsogolo mwake.

26 Ndipo upange mphete ziwiri zagolide, ndi kuzimanga pansonga zake ziwiri za chapachifuwa, m’mphepete mwake, m’katimo ku mbali ya kuefodi.

27 Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndi kuzimanga pa zapamapewa ziwiri za efodi, m’munsi, ku mbali yake ya kutsogolo, pafupi pa msoko wake, pamwamba pa mpango wa efodi.

28 Ndipo amange chapachifuwa pa mphete zake ndi mphete za efodi ndi mkuzi wamadzi, kuti chikhale pa mpango wa efodi; ndi kuti chapachifuwa chisamasuke paefodi.

29 Ndipo Aroni azinyamula maina a ana a Israele pa chapachifuwa cha chiweruzo pamtima pake, pakulowa iye m’malo opatulika, akhale chikumbutso pankhope pa Yehova kosalekeza.

30 Ndipo uikeUrimu ndi Tumimumwa chapachifuwa cha chiweruzo; ndipo zikhale pa mtima wa Aroni, pakulowa iye pamaso pa Yehova; ndipo Aroni azinyamula chiweruzo cha ana a Israele pamtima pake pamaso pa Yehova kosalekeza.

31 Ndipo uombe mwinjiro wa efodi ndi lamadzi lokha.

32 Ndipo polowa mutu pakhale pakati pake; pakhale mkawo pozungulira polowa pake, wa ntchito yoomba, ngati polowa pa malaya otchinjiriza, pangang’ambike.

33 Ndipo pa mbinyiru wake upange makangaza a lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, pambinyiru pake pozungulira, ndi kuwapakiza ndi miliu yagolide pozungulira;

34 mliu wa golide ndi khangaza, mliu wagolide ndi khangaza, pa mbinyiru wa mwinjiro pozungulira.

35 Ndipo Aroni auvale kuti atumikire nao; ndipo limveke liu lake pakulowa iye m’malo opatulika pamaso pa Yehova, ndi pakutuluka iye, kuti asafe.

Za golide waphanthiphanthi

36 Ndipo upange golide waphanthiphanthi woona, ndi kulochapo, monga malochedwe a chosindikizira, Kupatulikira Yehova.

37 Nuchiike pamkuzi wamadzi, ndipo chikhale panduwira, chikhale patsogolo pake pa nduwira.

38 Ndipo chizikhala pamphumi pake pa Aroni, ndipo Aroni azinyamula mphulupulu ya zopatulidwa, zimene ana a Israele azipatulira, ndi zopereka zao zonse zopatulira; ndipo chizikhala pamphumi pake kosalekeza, kuti alandiridwe pamaso pa Yehova.

39 Ndipo upikule malaya am’kati abafuta a thonje losansitsa, nusoke nduwira wabafuta, nusokenso mpango wopikapika.

40 Ndipo usokere ana a Aroni malaya am’kati, nuwasokere mipango; uwasokerenso akapa akhale aulemerero ndi okoma.

41 Ndipo uveke nazo Aroni mbale wako, ndi ana ake omwe; ndi kuwadzoza, ndi kudzaza dzanja lao, ndi kuwapatula, andichitire Ine ntchito ya nsembe.

42 Uwasokerenso zovala za miyendo za bafuta wa thonje losansitsa kubisa maliseche ao; ziyambire m’chuuno zifikire kuntchafu.

43 Ndipo azivale Aroni ndi ana ake, pakulowa iwo kuchihema chokomanako, kapena poyandikiza iwo kuguwa la nsembe kutumikira m’malo opatulika; anganyamule mphulupulu, nangafe; likhale lemba losatha la iye ndi mbumba zake pambuyo pake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/28-b7fb7f66d6f1e42a9c59014c31449b4f.mp3?version_id=1068—

Categories
EKSODO

EKSODO 29

Mapatulidwe a ansembe

1 Ichi ndicho uwachitire kuwapatula, andichitire ntchito ya nsembe: tenga ng’ombe yamphongo, ndi nkhosa ziwiri zamphongo zangwiro,

2 ndi mkate wopanda chotupitsa, ndi timitanda topanda chotupitsa tosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda taphanthi topanda chotupitsa, todzoza ndi mafuta; utipange ndi ufa wosalala watirigu.

3 Ndipo uziike mu dengu limodzi, ndi kubwera nazo mudengu, pamodzi ndi ng’ombe yamphongo ndi nkhosa ziwiri zamphongo.

4 Ndipo ubwere nao Aroni ndi ana ake aamuna ku khomo lachihema chokomanako, ndi kuwasambitsa m’madzi.

5 Pamenepo utenge zovalazo ndi kuveka Aroni malaya am’kati, ndi mwinjiro waefodi, ndi efodi, ndi chapachifuwa, ndi kummangira m’chuuno ndi mpango wa efodi woluka mwanzeru;

6 ndipo uike nduwira pamutu pake, ndi kuika korona wopatulika panduwirapo.

7 Pamenepo utenge mafuta odzoza nao nuwatsanulire pamutu pake, ndi kumdzoza.

8 Ndipo ubwere nao ana ake aamuna ndi kuwaveka malaya am’kati.

9 Uwamangirenso Aroni ndi ana ake aamuna mipango m’chuuno mwao, nuwamangire akapa pamutu pao; ndipo akhale ansembe mwa lemba losatha; nudzaze dzanja la Aroni ndi dzanja la ana ake aamuna.

10 Ndipo ubwere nayo ng’ombe yamphongo patsogolo pa chihema chokomanako; ndipo Aroni ndi ana ake aamuna aike manja ao pamutu pa ng’ombe yamphongoyo.

11 Nuphe ng’ombe yamphongoyo pamaso pa Yehova, pa khomo la chihema chokomanako.

12 Pamenepo utapeko pa mwazi wa ng’ombe yamphongo, ndi kuupaka pa nyanga za guwa la nsembe ndi chala chako, nutsanulire mwazi wonse pa tsinde la guwa la nsembe.

13 Nutenge mafuta onse akukuta matumbo, ndi chokuta cha mphafa ndi impso ziwiri, ndi mafuta ali pa izo, ndi kuzitentha paguwa la nsembe.

14 Koma nyama ya ng’ombeyo, ndi chikopa chake, ndi chipwidza chake, uzitentha izi ndi moto kunja kwa chigono; ndiyo nsembe yauchimo.

15 Utengenso nkhosa yamphongo imodziyo; ndi Aroni ndi ana ake aamuna aike manja ao pamutu pa nkhosa yamphongoyo.

16 Nuiphe nkhosa yamphongoyo, ndi kutenga mwazi wake, ndi kuuwaza paguwa la nsembe pozungulira.

17 Ndipo upadzule nkhosa yamphongo m’ziwalo zake, ndi kutsuka matumbo ake, ndi miyendo yake, ndi kuziika pa ziwalo zake, ndi pamutu pake.

18 Pamenepo upsereze nkhosa yamphongo yonse paguwa la nsembe; ndiyo nsembe yopsereza ya Yehova, ya fungo lokoma; ndiyo nsembe yamoto ya Yehova.

19 Ndipo utenge nkhosa yamphongo yinayo; ndi Aroni ndi ana ake aamuna aike manja ao pamutu pa nkhosa yamphongoyo.

20 Pamenepo uiphe nkhosa yamphongoyo, nutapeko pa mwazi wake, ndi kuupaka pa ndewerere ya khutu lamanja la Aroni, ndi pa ndewerere ya khutu lamanja ana ake aamuna, ndi pa chala chachikulu cha dzanja lao lamanja, ndi pa chala chachikulu cha phazi lao lamanja ndi kuuwaza mwaziwo paguwa la nsembe posungulira.

21 Ndipo utapeko pamwazi uli paguwa la nsembe, ndi pa mafuta akudzoza nao, ndi kuwaza pa Aroni, ndi pa zovala zake, ndi pa ana ake aamuna, ndi pa zovala za ana ake aamuna, pamodzi ndi iye; kuti akhale wopatulidwa, ndi zovala zake zomwe, ndi ana ake aamuna ndi zovala zao zomwe pamodzi ndi iye.

22 Utengenso mafuta a nkhosa yamphongoyo, ndi mchira, chokuta cha mphafa, ndi impso ziwiri, ndi mafuta ali pamenepo, ndi mwendo wam’mwamba wa ku dzanja lamanja; pakuti ndiyo nkhosa yamphongo ya kudzaza manja;

23 ndi mkate wamphumphu umodzi, ndi kamtanda ka mkate wosakaniza ndi mafuta, ndi kamtanda kamodzi kaphanthi, zili mu dengu la mkate wopanda chotupitsa wokhala pamaso pa Yehova;

24 ndipo uike zonsezi m’manja a Aroni, ndi m’manja a ana ake aamuna; nuziweyule nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.

25 Pamenepo uzilandire m’manja mwao, ndi kuzipsereza paguwa la nsembe, pa nsembe yopsereza, zichite fungo lokoma pamaso pa Yehova; ndiyo nsembe yamoto ya Yehova.

26 Ndipo utenge nganga ya nkhosa yamphongo yodzaza manja ya Aroni, ndi kuiweyula ikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ndipo ikhale gawo lako.

27 Ndipo upatule nganga ya nsembe yoweyula, ndi mwendo wam’mwamba wa nsembe yokweza, imene anaiweyula, ndi imene anaikweza, za nkhosa yamphongo yakudzaza manja; zili za Aroni, ndi za ana ake aamuna;

28 ndipo zikhale za Aroni ndi za ana ake aamuna, mwa lemba losatha, ziwadzere kwa ana a Israele; popeza ndiyo nsembe yokweza; ndipo ikhale nsembe yokweza yodzera kwa ana a Israele, ya kwa nsembe zamtendere zao, ndiyo nsembe yao yokweza ya Yehova.

29 Ndipo zovala zopatulika za Aroni zikhale za ana ake aamuna pambuyo pake, kuti awadzoze atazivala, nadzaze manja ao atazivala;

30 mwana wake wamwamuna amene adzakhala wansembe m’malo mwake azivala masiku asanu ndi awiri, pakulowa iye m’chihema chokomanako kutumikira m’malo opatulika.

31 Ndipo utenge nkhosa yamphongo yodzaza manja, nuphike nyama yake m’malo opatulika.

32 Ndipo Aroni ndi ana ake aamuna adye nyama ya nkhosa yamphongoyo, ndi mkate uli mudengu, pa khomo la chihema chokomanako.

33 Ndipo adye zimene anachita nazo choteteza, kuti awadzaze manja ndi kuwapatulitsa; koma mlendo asadyeko, pakuti nzopatulika izi.

34 Ndipo ikatsalako nyama yodzaza manja, kapena mkate kufikira m’mawa, pamenepo utenthe zotsalazo ndi moto; asazidye popeza nchopatulika ichi.

35 Ndipo utero nao Aroni, ndi ana ake aamuna, monga mwa zonse ndakuuza; udzaze manja ao masiku asanu ndi awiri.

36 Nukonze ng’ombe yamphongo, ndiyo nsembe yauchimo yakuteteza nayo, tsiku ndi tsiku; ndipo uyeretsa guwa la nsembe, pakuchita choteteza pamenepo; ndipo ulidzoze kulipatula.

37 Uchitire guwa la nsembe choteteza masiku asanu ndi awiri ndi kulipatula; ndipo guwa la nsembelo likhale lopatulika kwambiri; chilichonse chikhudza guwa la nsembelo chikhale chopatulika.

Nsembe ya masiku onse

38 Koma izi ndizo uzikonza paguwa la nsembelo; anaankhosa awiri a chaka chimodzi, tsiku ndi tsiku kosalekeza.

39 Mwanawankhosawina ukonze m’mawa; ndi mwanawankhosa wina ukonze madzulo;

40 ndi pa mwanawankhosa mmodziyo pakhale limodzi la magawo khumi la ufa wosalala, wosakaniza ndi limodzi la magawo anai la hini wa mafuta opera; ndi limodzi la magawo anai la hini wa vinyo, likhale nsembe yothira.

41 Ndi mwanawankhosa wina ukonze madzulo; umkonze umo unachitira nsembe yaufa cha m’mawa ndi nsembe yake yothira, akhale fungo lokoma, nsembe yamoto ya Yehova.

42 Ikhale nsembe yopsereza yosalekeza ya mwa mibadwo yanu, pa khomo la chihema chokomanako, pamaso pa Yehova, kumene ndidzakomana nanu, kulankhula nawe komweko.

43 Ndipo pamenepo ndidzakomana ndi ana a Israele; ndipo chihema chidzapatulidwa ndi ulemerero wanga.

44 Ndipo ndidzapatula chihema chokomanako, ndi guwa la nsembe; ndidzapatulanso Aroni ndi ana ake aamuna omwe, andichitire ntchito ya nsembe.

45 Ndipo ndidzakhala pakati pa ana a Israele, ndi kukhala Mulungu wao.

46 Ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wao, amene ndinawatulutsa m’dziko la Ejipito, kuti ndikhale pakati pao. Ine ndine Yehova Mulungu wao.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EXO/29-93258c3d3ed363f80d63cca94d51cbc5.mp3?version_id=1068—