Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 30

Mulungu alonjeza kuwalanditsa akalapa atachimwa

1 Ndipo kudzakhala, zikakugwerani zonsezi, mdalitso ndi temberero, ndinaikazi pamaso panu, ndipo mukazikumbukira mumtima mwanu mwaamitunduonse, amene Yehova Mulungu wanu anakupirikitsiraniko;

2 nimukabwerera kwa Yehova Mulungu wanu, ndi kumvera mau ake, monga mwa zonse ndikuuzani lero lino, inu ndi ana anu, ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse;

3 pamenepo Yehova Mulungu wanu adzauchotsa ukapolo wanu, ndi kukuchitirani chifundo; nadzabwera ndi kukumemezani mwa mitundu yonse ya anthu, kumene Yehova Mulungu wanu anakubalalitsiraniko.

4 Otayika anu akakhala ku malekezero a thambo, Yehova Mulungu wanu adzakumemezani kumeneko, nadzakutenganiko;

5 ndipo Yehova Mulungu wanu adzakulowetsani m’dziko lidakhala laolao la makolo anu, nilidzakhala lanulanu; ndipo adzakuchitirani zokoma, ndi kukuchulukitsani koposa makolo anu.

6 Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudulani mtima wanu, ndi mtima wa mbeu zanu, kuti mukonde Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, kuti mukhale ndi moyo.

7 Ndipo Yehova Mulungu wanu adzaika matemberero awa onse pa adani anu, ndi iwo akukwiya ndi inu, amene anakulondolani.

8 Pamenepo mutembenuke ndi kumvera mau a Yehova, ndi kuchita malamulo ake onse amene ndikuuzani lero lino.

9 Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakuchulukitsirani ntchito zonse za dzanja lanu, zipatso za thupi lanu, ndi zipatso za zoweta zanu, ndi zipatso za nthaka yanu, zikukomereni; popeza Yehova Mulungu wanu adzakondweranso kukuchitirani zokoma; monga anakondwera ndi makolo anu;

10 ngati mudzamvera mau a Yehova Mulungu wanu, kuwasunga malamulo ake ndi malemba ake olembedwa m’buku la chilamulo ichi; ngati mudzabwerera kudza kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse.

11 Pakuti lamulo ili ndikuuzani lero lino, silikukanikani kulizindikira, kapena silikhala kutali.

12 Silikhala m’mwamba, kuti mukati, Adzatikwerera m’mwamba ndani, ndi kubwera nalo kwa ife, ndi kutimvetsa ili, kuti tilichite?

13 Ndipo silikhala tsidya la nyanja, kuti mukati, Adzatiolokera ndani tsidya la nyanja, ndi kutitengera ili, ndi kutimvetsa ili, kuti tilichite?

14 Pakuti mauwa ali pafupifupi ndi inu, m’kamwa mwanu, ndi m’mtima mwanu, kuwachita.

15 Tapenyani, ndaika pamaso panu lero lino moyo ndi zokoma, imfa ndi zoipa;

16 popeza ndikuuzani lero kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda m’njira zake, ndi kusunga malamulo ake ndi malemba ake ndi maweruzo ake, kuti mukakhale ndi moyo ndi kuchuluka, ndi kuti Yehova Mulungu wanu akakudalitseni m’dziko limene mulowako kulilandira.

17 Koma mukatembenukira mtima wanu, osamvera inu, nimukacheteka, ndi kugwadira milungu ina ndi kuitumikira;

18 ndikulalikirani inu lero, kuti mudzatayika ndithu, masiku anu sadzachuluka m’dziko limene muolokera Yordani kulowamo kulilandira.

19 Ndichititsa mboni lero, kumwamba ndi dziko lapansi zitsutse inu; ndaika pamaso panu moyo ndi imfa, mdalitso ndi temberero; potero, sankhani moyo, kuti mukhale ndi moyo, inu ndi mbeu zanu;

20 kukonda Yehova Mulungu wanu, kumvera mau ake, ndi kummamatira Iye, pakuti Iye ndiye moyo wanu, ndi masiku anu ochuluka; kuti mukhale m’dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo, kuwapatsa ili.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/30-e69e4a14f58e9ffff03c49e146de16af.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 31

Yoswa adzalowa m’malo a Mose

1 Ndipo Mose anamuka nanena mau awa kwa Israele wonse,

2 nati nao, Ndine munthu wa zaka zana ndi makumi awiri lero lino; sindikhozanso kutuluka ndi kulowa; ndipo Yehova anati kwa ine, Sudzaoloka Yordani uyu.

3 Yehova Mulungu wanu ndiye adzaoloka pamaso panu, Iye ndiye adzaonongaamitunduawo pamaso panu, ndipo mudzawalandira. Yoswa ndiye adzakutsogolerani pooloka, monga ananena Yehova.

4 Ndipo Yehova adzawachitira monga anachitira Sihoni ndi Ogi, mafumu a Aamori, ndi dziko lao limene analiononga.

5 Yehova akadzawapereka pamaso panu, muziwachitira monga mwa lamulo lonse ndakuuzani.

6 Khalani amphamvu, limbikani mitima, musamachita mantha, kapena kuopsedwa chifukwa cha iwowa; popeza Yehova Mulungu wanu ndiye amene amuka nanu; Iye sadzakusowani, kapena kukusiyani.

7 Ndipo Mose anaitana Yoswa, nati naye pamaso pa Israele wonse, Khala wamphamvu, nulimbe mtima; pakuti udzalowa nao anthu awa m’dziko limene Yehova analumbirira makolo ao kuwapatsa ilo; ndipo iwe udzawalandiritsa ilo.

8 Ndipo Yehova, Iye ndiye amene akutsogolera; Iye adzakhala ndi iwe, Iye sadzakusowa kapena kukusiya; usamachita mantha, usamatenga nkhawa.

Pakutha zaka 7 zilizonse azilalikira chilamulocho

9 Ndipo Mose analembera chilamulo ichi, nachipereka kwa ansembe, ana a Levi, akunyamulalikasa la chipanganola Yehova, ndi kwa akulu onse a Israele.

10 Ndipo Mose anawauza, ndi kuti, Pakutha pake pa zaka zisanu ndi ziwiri, pa nyengo yoikika ya m’chaka chakulekerera, pachikondwerero cha Misasa;

11 pakufika Israele wonse kuoneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, m’malo amene adzasankha, muzilalikira chilamulo ichi pamaso pa Israele wonse, m’makutu mwao.

12 Sonkhanitsani anthu, amuna ndi akazi ndi ana aang’ono, ndi mlendo wokhala m’midzi mwanu, kuti amve, ndi kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu, ndi kusamalira kuchita mau onse a chilamulo ichi;

13 ndi kuti ana ao osadziwa amve, naphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu, masiku onse akukhala ndi moyo inu kudziko kumene muolokera Yordani kulilandira likhale lanulanu.

Yoswa asenza udindo wake

14 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Taona, ayandikira masiku ako akuti uyenera kufa; kaitane Yoswa, nimuoneke m’chihema chokomanako, kuti ndimlangize. Namuka Mose ndi Yoswa, naoneka m’chihema chokomanako.

15 Ndipo Yehova anaoneka m’chihema, m’mtambo njo; ndipo mtambo njo unaima pa khomo la chihema.

16 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Taona, udzagona tulo ndi makolo ako; ndi anthu awa adzauka, nadzatsata ndi chigololo milungu yachilendo ya dziko limene analowa pakati pake, nadzanditaya Ine, ndi kuthyola chipangano changa ndinapangana naocho.

17 Pamenepo ndidzawapsera mtima tsiku ilo, ndipo ndidzawataya, ndi kuwabisira nkhope yanga, ndipo adzathedwa, ndi zoipa ndi zovuta zambiri zidzawafikira; kotero kuti adzati tsiku lija, Sizitifikira kodi zoipa izi popeza Mulungu wathu sakhala pakati pa ife?

18 Koma Ine ndidzabisatu nkhope yanga tsiku lija chifukwa cha zoipa zonse adazichita; popeza anadzitembenukira milungu ina.

19 Ndipo tsopano mudzilemberere nyimbo iyi, ndi kuphunzitsa ana a Israele iyi; muiike m’kamwa mwao, kuti nyimbo iyi indichitire mboni yotsutsa ana a Israele.

20 Pakuti nditakalowetsa awa m’dziko limene ndinalumbirira makolo ao, moyenda mkaka ndi uchi ngati madzi; ndipo atadya nakhuta, nanenepa, pamenepo adzatembenukira milungu ina, ndi kuitumikira, ndi kundipeputsa Ine, ndi kuthyola chipangano changa.

21 Ndipo kudzakhala, zitawafikira zoipa ndi zovuta zambiri, nyimbo iyi idzachita mboni pamaso pao; popeza siidzaiwalika m’kamwa mwa mbeu zao; popeza ndidziwa zolingirira zao azichita lero lino, ndisanawalowetse m’dziko limene ndinalumbira.

22 Potero Mose analembera nyimboyi tsiku lomweli, naiphunzitsa ana a Israele.

23 Ndipo anauza Yoswa mwana wa Nuni, nati Khala wamphamvu, nulimbe mtima; pakuti udzalowa nao ana a Israele m’dziko limene ndinawalumbirira; ndipo Ine ndidzakhala ndi iwe.

24 Ndipo kunali, Mose atatha kulembera mau a chilamulo ichi m’buku, kufikira atalembera onse,

25 Mose anauza Alevi akunyamulalikasa la chipanganola Yehova, ndi kuti,

26 Landirani buku ili la chilamulo, nimuliike pambali pa likasa la chipangano la Yehova Mulungu wanu, likhale komweko mboni yakutsutsa inu.

27 Pakuti ndidziwa kupikisana kwanu, ndi kupulukira kwanu; taonani, pokhala ndikali ndi moyo pamodzi ndi inu lero, mwapikisana ndi Yehova; koposa kotani nanga nditamwalira ine!

28 Ndisonkhanitsire akulu onse a mafuko anu, ndi akapitao anu, kuti ndinene mau awa m’makutu mwao, ndi kuchititsa mboni kumwamba ndi dziko lapansi zitsutse iwo.

29 Pakuti ndidziwa kuti nditamwalira ine mudzadziipsa ndithu, ndi kupatuka m’njira imene ndinakuuzani; ndipo chidzakugwerani choipa masiku otsiriza; popeza mudzachita choipa pamaso pa Yehova, kuutsa mkwiyo wake ndi ntchito za manja anu.

30 Ndipo Mose ananena mau a nyimbo iyi m’makutu mwa msonkhano wonse wa Israele, kufikira adatha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/31-f7f71b085bb57e8260aceabdd5902ca0.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 32

Nyimbo adailemba Mose

1 Kumwamba kutchere khutu,

ndipo ndidzanena;

ndi dziko lapansi limve mau a m’kamwa mwanga.

2 Chiphunzitso changa chikhale ngati mvula;

maneno anga agwe ngati mame;

ngati mvula yowaza pamsipu,

ndi monga madontho a mvula pazitsamba.

3 Pakuti ndidzalalika dzina la Yehova.

Nenani kuti Mulungu wathu ndi wamkulu.

4 Thanthwe, ntchito yake ndi yangwiro;

pakuti njira zake zonse ndi chiweruzo;

Mulungu wokhulupirika ndi wopanda chisalungamo;

Iye ndiye wolungama ndi wolunjika.

5 Anamchitira zovunda si ndiwo ana ake, chilema nchao;

iwo ndiwo mbadwo wopulukira ndi wokhotakhota.

6 Kodi mubwezera Yehova chotero,

anthu inu opusa ndi opanda nzeru?

Kodi si ndiye Atate wanu, Mbuye wanu;

anakulengani, nakukhazikitsani?

7 Kumbukirani masiku akale,

zindikirani zaka za mibadwo yambiri;

funsani atate wanu, adzakufotokozerani;

akulu anu, adzakuuzani.

8 Pamene Wam’mwambamwamba anagawiraamitunducholowa chao,

pamene anagawa ana a anthu,

anaika malire a mitundu ya anthu,

monga mwa kuwerenga kwao kwa ana a Israele.

9 Pakuti gawo la Yehova ndilo anthu ake;

Yakobo ndiye muyeso wa cholowa chake.

10 Anampeza m’dziko la mabwinja,

m’chipululu cholira chopanda kanthu;

anamzinga, anamlangiza,

anamsunga ngati kamwana ka m’diso.

11 Monga mphungu ikasula chisa chake,

nikapakapa pa ana ake,

Iye anayala mapiko ake, nawalandira,

nawanyamula pa mapiko ake.

12 Yehova yekha anamtsogolera,

ndipo palibe mulungu wachilendo naye.

13 Anamuyendetsa pa misanje ya dziko lapansi,

ndipo anadya zipatso za m’minda;

namyamwitsa uchi wa m’thanthwe,

ndi mafuta m’mwala wansangalabwe;

14 mafuta a mkaka wang’ombe, ndi mkaka wankhosa,

ndi mafuta a anaankhosa,

ndi nkhosa zamphongo za mtundu wa ku Basani, ndi atonde,

ndi impso zonenepa zatirigu;

ndipo munamwa vinyo, mwazi wamphesa.

15 Koma Yesuruni anasanduka wonenepa, natazira;

wasanduka wonenepa, wakula, wakuta ndi mafuta;

pamenepo anasiya Mulungu amene anamlenga,

napeputsa thanthwe la chipulumutso chake.

16 Anamchititsa nsanje ndi milungu yachilendo,

anautsa mkwiyo wake ndi zonyansa.

17 Anaziphera nsembe ziwanda, si ndizo Mulungu ai;

milungu yosadziwa iwo,

yatsopano yofuma pafupi,

imene makolo anu sanaiope.

18 Mwaleka Thanthwe limene linakubalani,

mwaiwala Mulungu amene anakulengani.

19 Ndipo Yehova anachiona, nawanyoza,

pakuipidwa nao ana ake aamuna, ndi akazi.

20 Ndipo Iye anati, Ndidzawabisira nkhope yanga,

ndidzaona kutsiriza kwao;

popeza iwo ndiwo mbadwo wopulukira,

ana osakhulupirika iwo.

21 Anautsa nsanje yanga ndi chinthu chosati Mulungu;

anautsa mkwiyo wanga ndi zopanda pake zao.

Ndidzautsa nsanje yao ndi iwo osakhala mtundu wa anthu;

ndidzautsa mkwiyo wao ndi mtundu wa anthu opusa.

22 Pakuti wayaka moto mu mkwiyo wanga,

utentha kumanda kunsi

ukutha dziko lapansi ndi zipatso zake,

nuyatsa maziko a mapiri.

23 Ndidzawaunjikira zoipa;

ndidzawathera mivi yanga.

24 Adzaonda nayo njala

adzanyekeka ndi makala a moto, chionongeko chowawa;

ndipo ndidzawatumizira mano a zilombo,

ndi ululu wa zokwawa m’fumbi.

25 Pabwalo lupanga lidzalanda,

ndi m’zipinda mantha;

lidzaononga mnyamata ndi namwali,

woyamwa pamodzi ndi munthu waimvi.

26 Ndinati, Ndikadawauzira ndithu,

ndikadafafaniza chikumbukiro chao mwa anthu.

27 Ndikadapanda kuopa mkwiyo wa pa mdani,

angayese molakwa outsana nao,

anganene, Lakwezeka dzanja lathu,

ndipo Yehova sanachite ichi chonse.

28 Popeza iwo ndiwo mtundu wa anthu wosowa uphungu konse,

ndipo alibe chidziwitso.

29 Akadakhala nazo nzeru, akadazindikira ichi,

akadasamalira chitsirizo chao!

30 Mmodzi akadapirikitsa zikwi,

awiri akadathawitsa zikwi khumi,

akadapanda kuwagulitsa Thanthwe lao,

akadapanda kuwapereka Yehova.

31 Popeza thanthwe lao nlosanga Thanthwe lathu,

oweruza a pamenepo ndiwo adani athu.

32 Pakuti mpesa wao ndiwo wa ku Sodomu,

ndi wa m’minda ya ku Gomora;

mphesa zao ndizo mphesa zandulu,

matsangwi ao ngowawa.

33 Vinyo wao ndiwo ululu wa zinjoka,

ndi ululu waukali wa mphiri.

34 Kodi sichisungika ndi Ine,

cholembedwa chizindikiro mwa chuma changa chenicheni?

35 Kubwezera chilango nkwanga, kubwezera komwe,

pa nyengo ya kuterereka phazi lao;

pakuti tsiku la tsoka lao layandika,

ndi zinthu zowakonzeratu zifulumira kudza.

36 Popeza Yehova adzaweruza anthu ake,

nadzachitira nsoni anthu ake;

pakuona Iye kuti mphamvu yao yatha,

wosatsala womangika kapena waufulu.

37 Pamenepo adzati, Ili kuti milungu yao,

thanthwe limene anathawirako?

38 Imene inadya mafuta a nsembe zao zophera,

nimwa vinyo wa nsembe yao yothira?

Iuke nikuthandizeni, Ikhale pobisalapo panu.

39 Tapenyani tsopano kuti Ine ndine Iye,

ndipo palibe mulungu koma Ine;

ndipha Ine, ndikhalitsanso ndi moyo,

ndikantha, ndichizanso Ine;

ndipo palibe wakulanditsa m’dzanja langa.

40 Pakuti ndikweza dzanja langa kuloza kumwamba,

ndipo nditi, Pali moyo wanga kosatha,

41 ndikanola lupanga langa lonyezimira,

ndi dzanja langa likagwira chiweruzo;

ndidzabwezera chilango ondiukira,

ndi kulanga ondida.

42 Mivi yanga ndiiledzeretsa nao mwazi,

ndi lupanga langa lidzalusira nyama;

ndi mwazi wa ophedwa ndi ogwidwa,

ndi mutu wachitsitsi wa mdani.

43 Kondwerani, amitundu inu, ndi anthu ake;

adzalipsira mwazi wa atumiki ake,

adzabwezera chilango akumuukira,

nadzafafanizira zoipa dziko lake, ndi anthu ake.

44 Ndipo anadza Mose nanena mau onse a nyimbo iyi m’makutu mwa anthu, iye, ndi Yoswa mwana wa Nuni.

45 Ndipo Mose anatha kunena mau awa onse kwa Israele wonse;

46 nati nao, Ikani mitima yanu pa mau onse ndikuchitirani nao mboni lero; kuti muuze ana anu asamalire kuwachita mau onse a chilamulo ichi.

47 Pakuti sichikhala kwa inu chinthu chopanda pake, popeza ndicho moyo wanu, ndipo mwa chinthu ichi mudzachulukitsa masiku anu m’dziko limene muolokera Yordani, kulilandira.

Mulungu auza Mose akwere m’phiri la Nebo

48 Ndipo Yehova ananena ndi Mose tsiku lomweli, ndi kuti,

49 Kwera m’phiri muno mwa Abarimu, phiri la Nebo, lokhala m’dziko la Mowabu, popenyana ndi Yeriko; nupenye dziko la Kanani, limene ndipereka kwa ana a Israele likhale laolao;

50 nufe m’phiri m’mene ukweramo, nuitanidwe kunka kwa anthu a mtundu wako; monga Aroni mbale wako anafa m’phiri la Hori, naitanidwa kunka kwa anthu a mtundu wake;

51 popeza munandilakwira pakati pa ana a Israele ku madzi a Meriba wa Kadesi m’chipululu cha Zini, popeza simunandipatule Ine pakati pa ana a Israele.

52 Pakuti udzapenya dzikoli pandunji pako; koma osalowako ku dziko limene ndipatsa ana a Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/32-64b4de788f5560fb41ca5eb1e94c8e38.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 33

Mose adalitsa mafuko 12 a Israele asanafe

1 Ndipo mdalitso, Mose munthu wa Mulungu anadalitsa nao ana a Israele asanafe, ndi uwu.

2 Ndipo anati,

Yehova anafuma ku Sinai,

nawatulukira ku Seiri;

anaoneka wowala paphiri la Parani,

anafumira kwa opatulika zikwizikwi;

ku dzanja lamanja lake kudawakhalira lamulo lamoto.

3 Inde akonda mitundu ya anthu;

opatulidwa ake onse ali m’dzanja mwanu;

ndipo akhala pansi ku mapazi anu;

yense adzalandirako mau anu.

4 Mose anatiuza chilamulo,

cholowa cha msonkhano wa Yakobo.

5 Ndipo Iye anali mfumu mu Yesuruni,

pakusonkhana mafumu a anthu,

pamodzi ndi mafuko a Israele.

6 Rubeni akhale ndi moyo, asafe,

koma amuna ake akhale owerengeka.

7 Za Yuda ndi izi; ndipo anati,

Imvani, Yehova, mau a Yuda,

ndipo mumfikitse kwa anthu ake;

manja ake amfikire;

ndipo mukhale inu thandizo lake pa iwo akumuukira.

8 Ndipo za Levi anati,

Tumimu ndi Urimu wanu zikhala ndi wokondedwa wanu,

amene mudamuyesa mu Masa,

amene mudalimbana naye ku madzi a Meriba;

9 amene anati za atate wake ndi amai wake,

sindinamuone; Sanazindikire abale ake,

sanadziwe ana ake omwe;

popeza anasamalira mau anu,

nasungachipanganochanu.

10 Adzaphunzitsa Yakobo maweruzo anu,

ndi Israele chilamulo chanu;

adzaika chofukiza pamaso panu,

ndi nsembe yopsereza yamphumphu paguwa la nsembe lanu.

11 Dalitsani, Yehova, mphamvu yake,

nimulandire ntchito ya manja ake;

akantheni m’chuuno iwo akumuukira,

ndi iwo akumuda, kuti asaukenso.

12 Za Benjamini anati,

Wokondedwa wa Yehova adzakhala ndi Iye mokhazikika;

am’phimba tsiku lonse,

inde akhalitsa pakati pa mapewa ake.

13 Ndipo za Yosefe anati,

Yehova adalitse dziko lake;

ndi zinthu zofunikatu za m’mwamba, ndi mame,

ndi madzi okhala pansipo;

14 ndi zipatso zofunikatu za dzuwa,

ndi zomera zofunikatu za mwezi,

15 ndi zinthu zoposa za mapiri akale,

ndi zinthu zofunikatu za zitunda zosatha,

16 ndi zinthu zofunikatu za dziko lapansi, ndi kudzala kwake,

ndi chivomerezo cha Iye anakhala m’chitsambayo.

Mdalitso ufike pamutu wa Yosefe,

ndi pakati pamutu wake wa iye wokhala padera ndi abale ake.

17 Woyamba kubadwa wa ng’ombe yake,

ulemerero ndi wake;

nyanga zake ndizo nyanga zanjati;

adzatunga nazo mitundu ya anthu pamodzi,

kufikira malekezero a dziko lapansi.

Iwo ndiwo zikwi khumi za Efuremu,

iwo ndiwo zikwi za Manase.

18 Ndi za Zebuloni anati,

Kondwera, Zebuloni, ndi kutuluka kwako;

ndi Isakara, m’mahema mwako.

19 Adzaitana mitundu ya anthu afike kuphiri;

apo adzaphera nsembe za chilungamo;

popeza adzayamwa zochuluka za m’nyanja,

ndi chuma chobisika mumchenga.

20 Ndi za Gadi anati,

Wodala iye amene akuza Gadi;

akhala ngati mkango waukazi,

namwetula dzanja, ndi pakati pamutu pomwe.

21 Ndipo anadzisankhira gawo loyamba,

popeza kumeneko kudasungika gawo la wolamulira;

ndipo anadza ndi mafumu a anthu,

anachita chilungamo cha Yehova,

ndi maweruzo ake ndi Israele.

22 Ndi za Dani anati,

Dani ndiye mwana wa mkango,

wakutumpha motuluka mu Basani.

23 Za Nafutali anati,

Nafutali, wokhuta nazo zomkondweretsa,

wodzala ndi mdalitso wa Yehova;

landira kumadzulo ndi kumwera.

24 Ndi za Asere anati,

Asere adalitsidwe mwa anawo;

akhale wovomerezeka mwa abale ake,

aviike phazi lake m’mafuta.

25 Nsapato zako zikhale za chitsulo ndi mkuwa;

ndipo monga masiku ako momwemo mphamvu yako.

26 Palibe wina ngati Mulungu, Yesuruni iwe,

wakuyenda wokwera pathambo, kukuthandiza,

ndi pa mitambo mu ukulu wake.

27 Mulungu wamuyaya ndiye mokhaliramo mwako;

ndi pansipo pali manja osatha.

Ndipo aingitsa mdani pamaso pako,

nati, Ononga.

28 Ndipo Israele akhala mokhazikika pa yekha;

kasupe wa Yakobo;

akhala m’dziko la tirigu ndi vinyo;

inde thambo lake likukha mame.

29 Wodala iwe, Israele;

akunga iwe ndani, mtundu wa anthu opulumutsidwa ndi Yehova,

ndiye chikopa cha thandizo lako,

Iye amene akhala lupanga la ukulu wako!

Ndi adani ako adzakugonjera;

ndipo udzaponda pa misanje yao.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/33-96067d5fd0fea14c74ad5ef2c29a65a8.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 34

Imfa ya Mose

1 Ndipo Mose anakwera kuchokera ku zidikha za Mowabu, kunka kuphiri la Nebo, pamwamba pa Pisiga, popenyana ndi Yeriko. Ndipo Yehova anamuonetsa dziko lonse la Giliyadi, kufikira ku Dani;

2 ndi Nafutali lonse, ndi dziko la Efuremu, ndi Manase, ndi dziko lonse la Yuda, kufikira nyanja ya m’tsogolo;

3 ndi kumwera, ndi chidikha cha chigwa cha Yeriko, mzinda wa migwalangwa, kufikira ku Zowari.

4 Ndipo Yehova anati kwa iye, Si ili dziko ndinalumbirira Abrahamu, Isaki ndi Yakobo, ndi kuti, Ndidzalipereka kwa mbeu zako. Ndinakuonetsa ili m’maso, koma sudzaolokako.

5 Ndipo Mose mtumiki wa Yehova anamwalirako m’dziko la Mowabu, monga mwa mau a Yehova.

6 Ndipo Iye anamuika m’chigwa m’dziko la Mowabu popenyana ndi Betepeori; koma palibe munthu wakudziwa kumanda kwake kufikira lero lino.

7 Ndipo zaka zake za Mose ndizo zana limodzi ndi makumi awiri, pakumwalira iye; diso lake silinachite mdima, ndi mphamvu yake siidaleke.

8 Ndipo ana a Israele analira Mose m’zidikha za Mowabu masiku makumi atatu; potero anatha masiku akulira maliro a Mose.

9 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anadzala ndi mzimu wanzeru; popeza Mose adamuikira manja ake; ndi ana a Israele anamvera iye, nachita monga Yehova adauza Mose.

10 Ndipo sanaukensomnenerimu Israele ngati Mose, amene Yehova anadziwana naye popenyana maso;

11 kunena za zizindikiro ndi zozizwa zonse zimene Yehova anamtumiza kuzichita m’dziko la Ejipito kwaFarao, ndi anyamata ake onse, ndi dziko lake lonse;

12 ndi kunena za dzanja la mphamvu lonse, ndi choopsa chachikulu chonse, chimene Mose anachita pamaso pa Israele wonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/34-e47aa763f7e2ea0c553b6abb35a66127.mp3?version_id=1068—