Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 10

Za magome achiwiri a Malamulo

1 Masiku aja Yehova anati kwa ine, Dzisemere magome awiri amiyala onga oyamba aja, nukwere kuno kwa Ine m’phiri umu, nudzipangire likasa lamtengo.

2 Ndipo ndidzalembera pa magomewo mauwo anali pa magome oyamba aja amene unawaswa, ndipo uwaike m’likasamo.

3 Potero ndinapanga likasa la mtengo wakasiya, ndinasemanso magome awiri amiyala onga oyamba aja, ndi kukwera m’phirimo, magome awiri ali m’manja mwanga.

4 Ndipo analembera pamagome, monga mwa malembedwe oyamba, mau khumiwo, amene Yehova adanena ndi inu m’phirimo, ali pakati pa moto, tsiku la kusonkhanako; ndipo Yehova anandipatsa awa.

5 Ndipo ndinatembenuka ndi kutsika m’phiri, ndi kuika magome m’likasa ndinalipanga, ali m’menemo monga Yehova anandilamulira ine.

6 Ndipo ana a Israele anayenda ulendo wao kuchokera ku zitsime za ana a Yaakani kufikira ku Mosera. Kumeneko anamwalira Aroni, ndi kumeneko anamuika; ndipo Eleazara mwana wake anachita ntchito ya nsembe m’malo mwake.

7 Kuchokerako ananka ulendo ku Gudigoda, ndi kuchokera ku Gudigoda kunka ku Yotibata, dziko la mitsinje yamadzi.

8 Masiku aja Yehova anapatula fuko la Levi, linyamulelikasa la chipanganola Yehova, liimirire pamaso pa Yehova kumtumikira, ndi kudalitsa m’dzina lake kufikira lero lino.

9 Chifukwa chake Levi alibe gawo kapena cholowa pamodzi ndi abale ake; Yehova mwini wake ndiye cholowa chake, monga Yehova Mulungu wake ananena naye.

10 Ndipo ndinakhala m’phiri monga poyamba paja, masiku makumi anai usana ndi usiku; ndipo Yehova anandimvera ine pameneponso; Yehova sanafune kukuonongani.

11 Ndipo Yehova anati kwa ine, Uka, tenga ulendo pamaso pa anthu; kuti alowe ndi kulandira dzikoli ndinalumbirira makolo ao kuti ndidzawapatsa.

Abwereza kuwadandaulira akonde namvere Mulungu

12 Ndipo tsopano, Israele, Yehova Mulungu wanu afunanji nanu, koma kuti muziopa Yehova Mulungu wanu, kuyenda m’njira zake zonse, ndi kukonda, ndi kutumikira Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,

13 kusunga malamulo a Yehova, ndi malemba ake, amene ndikuuzani lero kuti kukukomereni inu?

14 Taonani thambo, ndi kumwambamwamba, dziko lapansi, ndi zonse zili m’mwemo ndi zake za Yehova Mulungu wanu.

15 Koma Yehova anakondwera nao makolo anu kuwakonda, nasankha mbeu zao zakuwatsata, ndiwo inu, mwa mitundu yonse ya anthu, monga kuli lero lino.

16 Potero dulani khungu la mitima yanu, ndipo musamapulukiranso.

17 Popeza Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu wa milungu, ndi Mbuye wa ambuye; Mulungu wamkulu, wamphamvu, ndi woopsa, wosasamalira nkhope za anthu, kapena kulandira chokometsera mlandu.

18 Aweruzira ana amasiye ndi mkazi wamasiye; ndipo akonda mlendo, ndi kumpatsa chakudya ndi chovala.

19 M’mwemo mukondane naye mlendo; popeza munali alendo m’dziko la Ejipito.

20 Muziopa Yehova Mulungu wanu; mumtumikire Iyeyo; mummamatire Iye, ndi kulumbira pa dzina lake.

21 Iye ndiye lemekezo lanu, Iye ndiye Mulungu wanu, amene anachita nanu zazikulu ndi zoopsa izi, mudaziona m’maso mwanu.

22 Makolo anu anatsikira ku Ejipito ndiwo anthu makumi asanu ndi awiri; ndipo Yehova Mulungu wanu anakusandulizani tsopano muchuluke ngati nyenyezi za kumwamba.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/10-03341179e6ea49ff4f9d57f3f0dda54d.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 11

1 Chifukwa chake muzikonda Yehova Mulungu wanu, ndi kusunga chilangizo chake, ndi malemba ake, ndi maweruzo ake, ndi malamulo ake, masiku onse.

2 Ndipo dziwani lero lino; pakuti sindinena ndi ana anu osadziwa, ndi osapenya kulanga kwa Yehova Mulungu wanu, ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, ndi mkono wake wotambasuka,

3 ndi zizindikiro zake, ndi ntchito zake, adazichitiraFaraomfumu ya Aejipito, ndi dziko lake lonse pakati pa Ejipito;

4 ndi chochitira Iye nkhondo ya Ejipito, akavalo ao, ndi agaleta ao; kuti anawamiza m’madzi a Nyanja Yofiira, muja anakutsatani m’mbuyo, ndi kuti Yehova anawaononga kufikira lero lino;

5 ndi chimene anakuchitirani m’chipululu, kufikira munadza kumalo kuno;

6 ndi chimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana a Eliyabu, mwana wa Rubeni; muja nthaka inatsegula pakamwa pake, ndi kuwameza iwo, ndi mabanja ao, ndi mahema ao, ndi za moyo zonse zakuwatsata pakati pa Israele wonse.

7 Koma maso anu anapenya ntchito yonse yaikulu ya Yehova anaichita.

8 Potero muzisunga malamulo onsewa ndikuuzani lero lino, kuti mukhale amphamvu, ndi kulowa ndi kulandira dziko, limene munkako kulilandira;

9 ndi kuti masiku anu achuluke m’dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, kuti adzawapatsa iwo ndi mbeu zao, dziko moyenda mkaka ndi uchi ngati madzi.

10 Pakuti dziko limene munkako kulilandira ndi losanga dziko la Ejipito lija mudatulukako, kumene kuja munafesa mbeu zanu, ndi kuzithirira ndi phazi lanu, monga munda watherere;

11 koma dziko limene munkako kulilandira ndilo dziko la mapiri ndi zigwa; limamwa madzi a mvula ya kumwamba;

12 ndilo dziko loti Yehova Mulungu wanu alisamalira, maso a Yehova Mulungu wanu akhalapo chikhalire, kuyambira chaka mpaka kutsiriza chaka.

Za madalitso otsatira kumvera kwao

13 Ndipo kudzakhala mukasamalira chisamalire malamulo anga amene ndikuuzani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kumtumikira ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse,

14 ndidzapatsa mvula ya dziko lanu m’nyengo yake, ya chizimalupsa ndi ya masika, kuti mutute tirigu wanu, ndi vinyo wanu, ndi mafuta anu.

15 Ndipo ndidzapatsa msipu wa zoweta zanu podyetsa panu; mudzadyanso nimudzakhuta.

16 Dzichenjerani nokha, angachete mitima yanu, nimungapatuke, ndi kutumikira milungu ina, ndi kuipembedza;

17 ndi kuti Mulungu angapse mtima pa inu, nangatseke kumwamba, kuti isowe mvula, ndi kuti nthaka isapereke zipatso zake; ndi kuti mungaonongeke msanga m’dziko lokomali Yehova akupatsani.

18 Chifukwa chake muzisunga mau anga awa mumtima mwanu ndi m’moyo mwanu; ndi kuwamanga ngati chizindikiro pamanja panu; ndipo zikhale zapamphumi pakati pamaso anu.

19 Ndipo muziwaphunzitsa ana anu, ndi kuwalankhula awa pokhala inu pansi m’nyumba mwanu, ndi poyenda inu panjira, ndi pogona inu pansi, ndi pakuuka inu pomwe.

20 Ndipo muziwalembera pa mphuthu za nyumba zanu, ndi pa zipata zanu;

21 kuti masiku anu ndi masiku a ana anu achuluke m’dziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzawapatsali, monga masiku a thambo lili pamwamba padziko.

22 Pakuti mukasunga chisungire malamulo awa onse amene ndikuuzani kuwachita; kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda m’njira zake zonse, ndi kummamatira;

23 Yehova adzapirikitsaamitunduawa onse pamaso panu, ndipo mudzalanda amitundu aakulu ndi amphamvu oposa inu.

24 Pamalo ponse padzapondapo phazi lanu ndi panu, kuyambira chipululu ndi Lebanoni, kuyambira pamtsinjewo, mtsinje wa Yufurate, kufikira nyanja ya m’tsogolo, ndiwo malire anu.

25 Palibe munthu adzaima pamaso panu; Yehova Mulungu wanu adzanjenjemeretsa ndi kuopsa dziko lonse mudzapondapo, chifukwa cha inu, monga anenana ndi inu.

Mdalitso ndi temberero

26 Taonani, ndilikuika pamaso panu lero dalitso ndi temberero;

27 dalitso, ngati mudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikuuzani lero lino;

28 koma temberero, ngati simudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi kupatuka m’njira ndikuuzani lero lino, kutsata milungu ina imene simunaidziwa.

29 Ndipo kudzakhala, atakulowetsani Yehova Mulungu wanu m’dziko limene munkako kulilandira, munene mdalitso paphiri la Gerizimu, ndi temberero paphiri la Ebala.

30 Sakhala kodi tsidya lija la Yordani, m’tseri mwake mwa njira yake yolowa dzuwa, m’dziko la Akanani, akukhala m’chidikha, pandunji pake pa Giligala, pafupi pa mathundu a More?

31 Pakuti mulinkuoloka Yordani kulowa ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani; ndipo mudzachilandira cholowa chanu, ndi kukhalamo.

32 Potero samalirani kuchita malemba ndi maweruzo onse ndiwaika pamaso panu lero lino.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/11-bddff0ff35d7252b84613849635eea54.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 12

Malo Oyera akhale amodzi

1 Awa ndi malemba ndi maweruzo, muziwasamalirawa kuwachita m’dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu anakupatsani likhale lanulanu, masiku onse akukhala ndi moyo inu padziko lapansi.

2 Muononge konse malo onse,amitunduamene mudzawalanda anatumikirako milungu yao, pa mapiri aatali, ndi pa zitunda, ndi pansi pa mitengo yonse yabiriwiri;

3 nimugumule maguwa ao a nsembe, ndi kuphwanya zoimiritsa zao, ndi kutentha zifanizo zao, ndi kulikha mafano osema a milungu yao; ndipo muononge dzina lao lichoke m’malomo.

4 Musamatero ndi Yehova Mulungu wanu.

5 Koma kumalo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha mwa mafuko anu onse kuikapo dzina lake, ndiko ku chokhalamo chake, muzifunako, ndi kufikako;

6 ndi kubwera nazo kumeneko nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zanu zophera, ndi magawo anu onse a magawo khumi, ndi nsembe yokweza ya dzanja lanu, ndi zowinda zanu, ndi nsembe zanu zaufulu, ndi zoyamba kubadwa za ng’ombe zanu, ndi za nkhosa ndi mbuzi zanu;

7 ndipo kumeneko muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kukondwera nazo zonse mudazigwira ndi dzanja lanu, inu ndi a pa banja lanu, m’mene Yehova Mulungu wanu anakudalitsani.

8 Musamadzichita monga mwa zonse tizichita kuno lero, yense kuchita chilichonse chiyenera m’maso mwake;

9 pakuti mpaka lero simunafikire mpumulo ndi cholowa, zimene Yehova Mulungu wanu adzakupatsani.

10 Koma mudzaoloka Yordani, ndi kukhala m’dziko limene Yehova Mulungu wanu akulandiritsani; ndipo adzakupumulitsani akulekeni adani anu onse pozungulirapo, ndipo mudzakhala mokhazikika.

11 Pamenepo padzakhala malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsako dzina lake, kumeneko muzibwera nazo zonse ndikuuzanizi; nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zanu zophera, magawo anu onse a magawo khumi, ndi nsembe yokweza dzanja lanu, ndi zowinda zanu zosankhika zimene muzilonjezera Yehova.

12 Ndipo mudzakondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi ana anu aamuna, ndi ana anu aakazi, ndi antchito anu aamuna, ndi antchito anu aakazi, ndi Mlevi ali m’midzi mwanu, popeza alibe gawo kapena cholowa pamodzi ndi inu.

13 Dzichenjerani nokha, musamapereka nsembe zanu zopsereza pamalo ponse upaona:

14 koma pamalo pamene Yehova adzasankha, mwa limodzi la mafuko anu, pamenepo muzipereka nsembe zanu zopsereza, ndi pamenepo muzichita zonse ndikuuzani.

15 Koma monga mwa chikhumbo chonse cha moyo wanu muiphe ndi kudya nyama m’midzi yanu yonse, monga mwa mdalitso wa Yehova Mulungu wanu anakupatsani; odetsa ndi oyera adyeko, monga yamphoyo ndi yangondo.

16 Mwazi wao wokha musamadya; muziuthira panthaka ngati madzi.

17 Simungathe kudya m’mudzi mwanu limodzi la magawo khumi la tirigu wanu, kapena la vinyo wanu, kapena la mafuta anu, kapena oyamba kubadwa a ng’ombe zanu kapena la nkhosa ndi mbuzi zanu, kapena zowinda zanu zilizonse muzilonjeza kapena nsembe zanu zaufulu, kapena nsembe yokweza ya m’dzanja lanu;

18 koma muzizidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu m’malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha, inu, ndi ana anu aamuna, ndi ana anu aakazi, ndi antchito anu aamuna, ndi antchito anu aakazi, ndi Mlevi ali m’mudzi mwanu; nimukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu m’zonse mudazigwira ndi dzanja lanu.

19 Dzichenjerani nokha, musataye Mlevi masiku onse akukhala inu m’dziko mwanu.

Za kudya nyama

20 Akadzakuza malire a dziko lanu Yehova Mulungu wanu, monga ananena ndi inu, ndipo mukadzati, Ndidye nyama, popeza moyo wanga ukhumba kudya nyama; mudye nyama monga umo monse ukhumba moyo wanu.

21 Malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kuikako dzina lake akakutanimphirani, muziphako ng’ombe zanu ndi nkhosa ndi mbuzi zanu zimene Yehova anakupatsani, monga ndinakuuzani, ndi kuzidya m’mudzi mwanu, monga umo monse ukhumba moyo wanu.

22 Koma monga umo amadya mphoyo ndi ngondo momwemo uzizidya; odetsa ndi oyera adyeko chimodzimodzi.

23 Koma mulimbikepo ndi kusadya mwaziwo; popeza mwazi ndiwo moyo, nimusamadya moyo pamodzi ndi nyama yake.

24 Musamadya uwu; muuthire pansi ngati madzi.

25 Musamadya uwu; kuti chikukomereni inu, ndi ana anu akudza m’mbuyo mwanu, pakuchita inu zoyenera pamaso pa Yehova.

26 Zopatulika zanu zokha zimene muli nazo, ndi zowinda zanu, muzitenge, ndi kupita nazo ku malo amene Yehova adzasankha;

27 ndipo mupereke nsembe zanu zopsereza, nyama zao ndi mwazi wao, paguwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu; ndipo athire mwazi wa nsembe zanu zophera paguwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyama yake muidye.

28 Samalirani ndi kumvera mau awa onse ndikuuzaniwa, kuti chikukomereni inu, ndi ana anu akudza m’mbuyo mwanu nthawi zonse, pochita inu zokoma ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

29 Pamene Yehova Mulungu wanu akadzadulatu amitundu pamaso panu, kumene mulowako kuwalandira, ndipo mutawalandira, ndi kukhala m’dziko lao,

30 dzichenjerani nokha mungakodwe ndi kuwatsata, ataonongeka pamaso panu; ndi kuti mungafunsire milungu yao, ndi kuti, Amitundu awa atumikira milungu yao bwanji? Ndichite momwemo inenso.

31 Musamatero ndi Yehova Mulungu wanu; pakuti zilizonse zinyansira Yehova, zimene azida Iye, iwowa anazichitira milungu yao; pakuti angakhale ana ao aamuna ndi ana ao aakazi awatentha m’moto, nsembe ya milungu yao.

32 Chilichonse ndikuuzani, muchisamalire kuchichita; musamaonjezako, kapena kuchepsako.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/12-7319adb3f78255ed6e7102d703727548.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 13

Achenjere nao owanyenga kuwapembedzetsa mafano

1 Akauka pakati pa inu mneneri, kapena wakulota maloto, nakakupatsani chizindikiro kapena chozizwa;

2 ndipo chizindikiro kapena chozizwa adanenachi chifika, ndi kuti, Titsate milungu ina, imene simunaidziwe, ndi kuitumikira;

3 musamamvera mau a mneneri uyu, kapena wolota maloto uyu; popeza Yehova Mulungu wanu akuyesani, kuti adziwe ngati mukonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse.

4 Muziyenda kutsata Yehova Mulungu wanu, ndi kumuopa, ndi kusunga malamulo ake, ndi kumvera mau ake, ndi kumtumikira Iye, ndi kummamatira.

5 Ndipo mneneriyo, kapena wolota malotoyo, mumuphe; popeza ananena chosiyanitsa ndi Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani m’dziko la Ejipito, nakuombolani m’nyumba ya ukapolo; kuti akucheteni mutaye njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani muziyendamo. Potero muzichotsa choipacho pakati pa inu.

6 Mbale wanu, ndiye mwana wa mai wanu, kapena mwana wanu wamwamuna, kapena mwana wanu wamkazi, kapena mkazi wa kumtima kwanu, kapena bwenzi lanu, ndiye ngati moyo wanuwanu, akakukakamizani m’tseri, ndi kuti, Tipite titumikire milungu ina, imene simunaidziwe, inu, kapena makolo anu;

7 ndiyo milungu ya mitundu ya anthu akuzungulira inu, akukhala pafupi pali inu, kapena akukhala patali pali inu, kuyambira malekezero a dziko lapansi kufikira malekezero ena a dziko lapansi;

8 musamavomerezana naye, kapena kumvera iye; diso lanu lisamchitire chifundo, kapena kumleka, kapena kumbisa;

9 koma muzimupha ndithu; liyambe dzanja lanu kukhala pa iye kumupha, ndi pamenepo dzanja la anthu onse.

10 Nimuzimponya miyala, kuti afe; popeza anayesa kukuchetani muleke Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani m’dziko la Ejipito, m’nyumba ya ukapolo.

11 Kuti Israele yense amve, ndi kuopa, ndi kusaonjeza kuchita choipa chotere chonga ichi pakati pa inu.

12 Ukamva za umodzi wa mizinda yanu, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani kukhalako, ndi kuti,

13 Amuna ena opanda pake anatuluka pakati pa inu, nacheta okhala m’mzinda mwao, ndi kuti, Timuke titumikire milungu ina, imene simunaidziwe;

14 pamenepo muzifunsira, ndi kulondola, ndi kufunsitsa; ndipo taonani, chikakhala choona, chatsimikizika chinthuchi, kuti chonyansa chotere chachitika pakati pa inu;

15 muzikanthatu okhala m’mzinda muja ndi lupanga lakuthwa; ndi kuononga konse, ndi zonse zili m’mwemo, ng’ombe zake zomwe, ndi lupanga lakuthwa.

16 Ndipo muzikundika zofunkha zake zonse pakati pakhwalala pake, nimutenthe ndi moto mzinda, ndi zofunkha zake zonse konse, pamaso pa Yehova Mulungu wanu; ndipo udzakhala mulu ku nthawi zonse; asaumangenso.

17 Ndipo pasamamatire padzanja panu kanthu ka chinthu choti chionongeke; kuti Yehova aleke mkwiyo wake waukali, nakuchitireni chifundo, ndi kukumverani nsoni, ndi kukuchulukitsani monga analumbirira makolo anu;

18 pakumvera inu mau a Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikuuzani lero lino, kuchita zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/13-6ddffa2d6d727e49c0b84354adcf0191.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 14

Za nyama yodyedwa ndi yosadyedwa

1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu; musamadzicheka, kapena kumeta tsitsi pakati pamaso chifukwa cha akufa.

2 Popeza ndinu mtundu wa anthu opatulikira Yehova Mulungu wanu, ndipo Yehova anakusankhani mukhale mtundu wa anthu wa pa wokha wa Iye yekha, mwa mitundu yonse ya anthu okhala pankhope padziko lapansi.

Za nyama zodyeka ndi zosadyeka ndi zakufa zodetsa munthu

3 Musamadya chonyansa chilichonse.

4 Nyamazi muyenera kumadya ndi izi: ng’ombe, nkhosa, ndi mbuzi,

5 ngondo, ndi nswala ndi mphoyo, ndi mphalapala, ndi ngoma, ndi nyumbu, ndi mbalale.

6 Ndipo nyama iliyonse yogawanika chiboda, nikhala yogawanikadi chiboda, nibzikula, imeneyo muyenera kudya.

7 Koma izi zokha simuyenera kuzidya mwa zobzikulazo, kapena zogawanika chiboda:ngamira, ndi kalulu, ndi mbira, popeza zibzikula, koma zosagawanika chiboda, muziyese zodetsa;

8 ndi nkhumba, popeza igawanika chiboda koma yosabzikula, muiyese yodetsa; musamadya nyama yao, musamakhudza mitembo yao.

9 Mwa zonse zili m’madzi muyenera kumadya izi: zilizonse zili nazo zipsepse ndi mamba, zimenezi muyenera kumadya;

10 koma zilizonse zopanda zipsepse kapena mamba musamadya; muziyese zonyansa.

11 Mbalame zosadetsa zonse muyenera kumadya.

12 Koma izi ndi zimene simuyenera kumadya: mphungu, ndi nkhwazi, ndi chikambi,

13 ndi kamtema, ndi mphamba, ndi muimba monga mwa mtundu wake;

14 ndi khwangwala aliyense monga mwa mtundu wake;

15 ndi nthiwatiwa, ndi chipudo, ndi kakowa, ndi kabawi monga mwa mtundu wake;

16 ndi nkhutukutu, ndi manchichi, ndi tsekwe;

17 ndi vuwo, ndi dembo, ndi nswankhono;

18 ndi indwa, ndi chimeza, monga mwa mtundu wake, ndi sadzu, ndi mleme.

19 Ndipo zokwawa zonse zakuuluka muziyesa zonyansa; musamazidya.

20 Mbalame zonse zosadetsa muyenera kumadya.

21 Musamadya chinthu chilichonse chitafa chokha; muzipereka icho kwa mlendo ali m’mudzi mwanu, achidye ndiye; kapena uchigulitse kwa mlendo; popeza ndinu mtundu wa anthu wopatulika wa Yehova Mulungu wanu. Musamaphika mwanawambuzi mu mkaka wa make.

Za limodzi mwa magawo khumi

22 Muzipereka ndithu limodzi la magawo khumi la zipatso zonse za mbeu zanu, zofuma kumunda, chaka ndi chaka.

23 Ndipo muzidye pamaso pa Yehova Mulungu wanu, m’malo m’mene asankhamo Iye, kukhalitsamo dzina lake; limodzi la magawo khumi la tirigu wanu, la vinyo wanu, ndi la mafuta anu, ndi oyamba kubadwa a ng’ombe zanu ndi a nkhosa ndi mbuzi zanu; kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.

24 Ndipo ikakutalikirani njira kotero kuti simungathe kulinyamula, popeza malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha, kuikapo dzina lake, akutanimphirani; atakudalitsani Yehova Mulungu wanu;

25 pamenepo mulisinthe ndalama, ndi kumanga ndalama ikhale m’dzanja mwanu, ndi kupita ku malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha;

26 ndipo mugule ndi ndalamazo chilichonse moyo wanu ukhumba, ng’ombe kapena nkhosa, kapena vinyo, kapena chakumwa cholimba, kapena chilichonse moyo wanu ukufunsani; nimudye pomwepo pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kukondwera, inu ndi a pabanja panu.

27 Koma Mlevi wokhala m’mudzi mwanu, musamamtaya, popeza alibe gawo kapena cholowa pamodzi ndi inu.

28 Pakutha pake pa zaka zitatu muzitulutsa magawo onse a magawo khumi a zipatso zanu za chaka icho, ndi kuwalinditsa m’mudzi mwanu;

29 ndipo abwere Mlevi, popeza alibe gawo kapena cholowa pamodzi ndi inu, ndi mlendo, ndi ana amasiye, ndi mkazi wamasiye, okhala m’mudzi mwanu, nadye nakhute; kuti Yehova Mulungu wanu akakudalitseni mu ntchito zonse za dzanja lanu muzichitazi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/14-d5027b84152eeaf612cc5914454236ba.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 15

Za chaka cha chilekerero

1 Pakutha pake pa zaka zisanu ndi ziwiri pakhale chilekerero.

2 Chilekererocho ndichi: okongoletsa onse alekerere chokongoletsa mnansi wake; asachifunse kwa mnansi wake, kapena mbale wake; popeza analalikira chilekerero cha Yehova.

3 Muyenera kuchifunsa kwa mlendo; koma chanu chilichonse chili ndi mbale wanu, dzanja lanu lichilekerere;

4 ndiko kuti pasakhale waumphawi mwa inu; pakuti Yehova adzakudalitsani kwambiri m’dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale cholowa chanuchanu;

5 chokhachi mumvere chimverere mau a Yehova Mulungu wanu, kuti musamalire kuchita malamulo awa onse amene ndikuuzani lero lino.

6 Popeza Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani, monga ananena nanu; ndipo mudzakongoletsaamitunduambiri, osakongola nokha; nimudzachita ufumu pa amitundu ambiri, koma iwo sadzachita ufumu pa inu.

Za aumphawi ndi akapolo

7 Akakhala ndi inu munthu waumphawi, ndiye wina wa abale anu, mu umodzi wa midzi yanu, m’dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, musakhakala mtima wanu, kapena kuumitsa dzanja lanu kukaniza mbale wanu waumphawi;

8 koma muzimtansira dzanja lanu ndithu ndi kumkongoletsa ndithu zofikira kusowa kwake, monga umo amasowa.

9 Dzichenjerani, mungakhale mau opanda pake mumtima mwanu, ndi kuti, Chayandika chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka cha chilekerero; ndipo diso lanu lingaipire mbale wanu waumphawi, osampatsa kanthu; ndipo iye angalirire inu kwa Yehova; ndipo mwa inu mungakhale tchimo.

10 Muzimpatsa ndithu, osawawa mtima wanu pompatsa; popeza, chifukwa cha ichi Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mu ntchito zanu zonse, ndi m’zonse muikapo dzanja lanu.

11 Popeza waumphawi salekana m’dziko, chifukwa chake ndikuuzani ndi kuti, Dzanja lanu mulitansire ndithu mbale wanu, ndi ozunzika anu, ndi aumphawi anu, a m’dziko mwanu.

Lamulo la pa kapolo

12 Mukagula mbale wanu, Muhebri wamwamuna kapena Muhebri wamkazi, ndipo adzakutumikira zaka zisanu ndi chimodzi; koma chaka chachisanu ndi chiwiri umlole achoke kwanu waufulu.

13 Ndipo pomlola iwe achoke kwanu waufulu, musamamlola achoke wopanda kanthu;

14 mumlemeze nazo za nkhosa ndi mbuzi zanu, ndi za popondera mphesa, ndi za mosungira vinyo; monga Yehova Mulungu wanu anakudalitsani mumninkhe uyu.

15 Ndipo mukumbukire kuti munali akapolo m’dziko la Ejipito, ndipo Yehova Mulungu wanu anakuombolani; chifukwa chake ndikuuzani ichi lero lino.

16 Ndipo kudzakhala, akanena ndi inu, Sindituluka kuchoka kwanu; popeza akonda inu ndi nyumba yanu, popeza kumkomera kwanu;

17 pamenepo muzitenga lisungulo, ndi kulipisa m’khutu mwake, kulikanikiza ndi chitseko, ndipo adzakhala kapolo wanu kosalekeza. Muzichitanso momwemo ndi adzakazi anu.

18 Musamayesa nchosautsa, pomlola akuchokereni waufulu; popeza anakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi monga wolipidwa wakulandira chowirikiza; potero Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani m’zonse muzichita.

Za nyama zoyamba kubadwa

19 Zazimuna zonse zoyamba kubadwa, zobadwa mwa ng’ombe zanu ndi mwa nkhosa ndi mbuzi zanu, muzizipatulira Yehova Mulungu wanu; musamagwiritsa ntchito yoyamba kubadwa mwa ng’ombe zanu, kapena kusenga yoyamba kubadwa ya nkhosa kapena mbuzi zanu.

20 Muzidye chaka ndi chaka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, m’malo amene Yehova adzasankha, inu ndi a m’banja mwanu.

21 Koma ikakhala nacho chilema, yotsimphina, kapena yakhungu, chilema chilichonse choipa, musamaiphera nsembe Yehova Mulungu wanu.

22 Muidye m’mudzi mwanu; odetsa ndi oyera aidye chimodzimodzi, monga mphoyo ndi nswala.

23 Mwazi wake wokha musamadya; muuthire pansi ngati madzi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/15-bcd08cdc637bff389094e25da9da2980.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 16

Zikondwerero za Paska, za Masabata, ndi za Misasa

1 Samalirani mwezi wa Abibu, kuti muzichitira Yehova Mulungu wanuPaska; popeza m’mwezi wa Abibu Yehova Mulungu wanu anakutulutsani m’dziko la Ejipito usiku.

2 Ndipo muziphera Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paska, ya nkhosa ndi ya ng’ombe, m’malo amene Yehova adzasankha kukhalitsamo dzina lake.

3 Musamadyera nayo mkate wa chotupitsa; masiku asanu ndi awiri mudyere nayo mkate wopanda chotupitsa, ndiwo mkate wa chizunziko popeza munatuluka m’dziko la Ejipito mofulumira; kuti mukumbukire tsiku lotuluka inu m’dziko la Ejipito masiku onse a moyo wanu.

4 Ndipo m’malire mwanu monse musaoneke chotupitsa masiku asanu ndi awiri; nyama yomwe muiphere nsembe tsiku loyamba madzulo, isatsaleko usiku wonse kufikira m’mawa.

5 Simuyenera kuphera nsembe ya Paska m’midzi yanu iliyonse, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani;

6 koma pamalo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsapo dzina lake, pamenepo muphere nsembe ya Paska, madzulo, polowa dzuwa, nyengo ya kutuluka inu mu Ejipito.

7 Ndipo muiphike ndi kuidya m’malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha; koma m’mawa mwake mubwerere kunka ku mahema anu.

8 Masiku asanu ndi limodzi muzidya mkate wopanda chotupitsa; ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri ndilo loletsa, la Yehova Mulungu wanu; musamagwira ntchito pamenepo.

9 Mudziwerengere masabata asanu ndi awiri; muyambe kuwerenga masabata asanu ndi awiri poyambira kusenga tirigu wachilili.

10 Ndipo muchitire Yehova Mulungu wanu chikondwerero cha Masabata, ndiwo msonkho waufulu wa dzanja lanu, umene mupereke monga Yehova Mulungu wanu akudalitsani.

11 Ndipo mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi ana anu aamuna, ndi ana anu aakazi, ndi antchito anu aamuna, ndi antchito anu aakazi, ndi Mlevi wokhala m’mudzi mwanu, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye, okhala pakati pa inu, m’malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsako dzina lake.

12 Ndipo mukumbukire kuti munali akapolo mu Ejipito; musamalire kuchita malemba awa.

13 Mudzichitirechikondwerero cha Misasamasiku asanu ndi awiri, mutasunga za padwale ndi za mopondera mphesa;

14 nimukondwere m’madyerero mwanu, inu, ndi ana anu aamuna, ndi ana anu aakazi, ndi antchito anu aamuna, ndi antchito anu aakazi, ndi Mlevi, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye okhala m’mudzi mwanu.

15 Masiku asanu ndi awiri muchitire Yehova Mulungu wanu madyerero m’malo amene Yehova adzasankha; popeza Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani m’zipatso zanu zonse, ndi m’ntchito zonse za manja anu; nimukondwere monsemo.

16 Amuna onse azioneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu m’malo amene Iye adzasankha, katatu m’chaka; pachikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa, pa chikondwerero cha masabata, ndi pa chikondwerero cha Misasa; ndipo asaoneke pamaso pa Yehova opanda kanthu;

17 apereke yense monga mwa mphatso ya m’dzanja lake, monga mwa mdalitso wa Yehova Mulungu wanu anakupatsani.

Za oweruza milandu

18 Mudziikire oweruza ndi akapitao m’midzi yanu yonse imene Yehova Mulungu wanu akupatsani, monga mwa mafuko anu; ndipo aweruze anthu ndi chiweruzo cholungama.

19 Musamapotoza chiweruzo, musamasamalira munthu, kapena kulandira chokometsera mlandu; popeza chokometsera mlandu chidetsa maso a anzeru, ndi kuipisa mau a olungama.

20 Chilungamo, chilungamo ndicho muzichitsata, kuti mukhale ndi moyo ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani.

21 Musazike kwa inu nokha mzati wa Ashera, wa mtengo uliwonse, pafupi pa guwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu, limene mwadzimangira.

22 Ndipo musamadziutsira choimiritsa chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu adana nacho.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/16-997a0d359e10e188987c9099fd406a04.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 17

1 Musamaphera Yehova Mulungu wanu nsembe ya ng’ombe, kapena nkhosa, yokhala nacho chilema, kapena chilichonse choipa; pakuti chinyansira Yehova Mulungu wanu.

2 Akapeza pakati panu, m’mudzi wanu wina umene anakupatsani Yehova Mulungu wanu, wamwamuna kapena wamkazi wakuchita chili choipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kulakwirachipanganochake,

3 nakatumikira milungu ina, naigwadira iyo, kapena dzuwa, kapena mwezi, kapena wina wa khamu la kuthambo, losauza Ine;

4 ndipo akakuuzani, nimudamva, pamenepo muzifunsira, ndipo taonani, chikakhala choonadi, choti nzenizeni, chonyansachi chachitika mu Israele;

5 pamenepo mutulutse mwamunayo kapena mkaziyo, anachita choipacho, kunka naye ku zipata zanu, ndiye wamwamuna kapena wamkazi; ndipo muwaponye miyala, kuti afe.

6 Pakamwa pa mboni ziwiri kapena zitatu amuphe iye amene akuti afe; asamuphe pakamwa pa mboni imodzi.

7 Liyambe kumgwera dzanja la mboniyo kumupha; pamenepo dzanja la anthu onse. Potero muzichotsa choipacho pakati panu.

8 Ukakukanikani mlandu pouweruza, ndiwo wakunena zamwazi, kapena zakutsutsana, kapena zakupandana, ndiyo milandu yakutengana m’midzi mwanu; pamenepo muziuka ndi kukwera kunka ku malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha;

9 nimufike kwa ansembe, Alevi, ndi kwa woweruza wa m’masiku awo; nimufunsire; ndipo adzakufotokozerani maweruzidwe ake.

10 Ndipo muchite monga momwe ananena mau akufotokozeraniwo, ku malo amene Yehova adzawasankha; nimusamalire kuchita monga mwa zonse akulangizanizi.

11 Monga momwe anena malamulo akulangizani, ndi monga mwa chiweruzo akufotokozerani muchite; mau akufotokozerani musawapatukire kulamanja kapena kulamanzere.

12 Koma munthu wakuchita modzikuza, osamvera wansembe wokhala chilili kutumikirako pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kapena woweruza, munthuyo afe; ndipo muchotse choipacho kwa Israele.

13 Ndipo anthu onse adzamva ndi kuchita mantha, osachitanso modzikuza.

Za kusankha mfumu ndi zomuyenera

14 Mutakalowa m’dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, ndi kulilandira lanulanu, ndi kukhalamo; ndipo mukanena, Tidziikire mfumu, mongaamitunduonse akutizinga;

15 mumuiketu mfumu yanu imene Yehova Mulungu wanu adzaisankha; wina pakati pa abale anu mumuike mfumu yanu; simuyenera kudziikira mlendo, wosakhala mbale wanu.

16 Koma asadzichulukitsire akavalo iye, kapena kubwereretsa anthu anke ku Ejipito, kuti achulukitse akavalo; popeza Yehova anati nanu, Musamabwereranso njira iyi.

17 Ndipo asadzichulukitsire akazi, kuti ungapatuke mtima wake; kapena asadzichulukitsire kwambirisilivandi golide.

18 Ndipo kudzali, pakukhala iye pa mpando wachifumu wa ufumu wake, adzilemberere chofanana cha chilamulo ichi m’buku, achitenge pa ichi chili pamaso pa ansembe Alevi;

19 ndipo azikhala nacho, nawerengemo masiku onse a moyo wake; kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake, kusunga mau onse a chilamulo ichi ndi malemba awa, kuwachita;

20 kuti mtima wake usadzikuze pa abale ake, ndi kuti asapatukire lamulolo, kulamanja kapena kulamanzere; kuti achuluke masiku ake, mu ufumu wake, iye ndi ana ake pakati pa Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/17-22c08d236d46ed9c611a617f5e3c0885.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 18

Zoyenera ansembe ndi Alevi

1 Ansembe Alevi, fuko lonse la Levi, alibe gawo kapena cholowa pamodzi ndi Israele; azizidya nsembe zamoto za Yehova, ndi cholowa chake.

2 Alibe cholowa pakati pa abale ao; Yehova mwini wake ndiye cholowa chao, monga ananena nao.

3 Ndipo zoyenera ansembe, awapatse anthu akuphera nsembe ndizo: ingakhale ng’ombe kapena nkhosa azipatsa wansembe mwendo wamwamba, ndi ya m’masaya ndi chifu.

4 Zipatso zoyamba za tirigu wanu, za vinyo wanu, ndi za mafuta anu ndi ubweya woyamba kuusenga, muwapatse izi.

5 Popeza Yehova Mulungu wanu anawasankha mwa mafuko anu onse, aimirire natumikire m’dzina la Yehova, iwo ndi ana ao aamuna kosalekeza.

6 Ndipo Mlevi akachokera kumudzi wanu wina mu Israele monse, kumene akhalako, nakadza ndi chifuniro chonse cha moyo wake ku malo amene Yehova adzasankha;

7 pamenepo azitumikira m’dzina la Yehova Mulungu wake, monga amachita abale ake onse Alevi akuimirirako pamaso pa Yehova.

8 Chakudya chao chizifanana, osawerengapo zolowa zake zogulitsa.

Mulungu aipidwa nao anyanga ndi obwebweta ndi onse otere

9 Mutakalowa m’dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, musamaphunzira kuchita monga mwa zonyansa zaamitunduaja.

10 Asapezeke mwa inu munthu wakupitiriza mwana wake wamwamuna kapena mwana wake wamkazi ku moto wa ula, wosamalira mitambo, kapena wosamalira kulira kwa mbalame, kapena wanyanga.

11 Kapena wotsirika, kapena wobwebweta, kapena wopenduza, kapena wofunsira akufa.

12 Popeza aliyense wakuchita izi Yehova anyansidwa naye; ndipo chifukwa cha zonyansa izi Yehova Mulungu wanu awapirikitsa pamaso panu.

13 Mukhale angwiro ndi Yehova Mulungu wanu.

14 Pakuti amitundu awa amene mudzawalandira, amamvera iwo akuyesa mitambo, ndi a ula; koma inu, Yehova Mulungu wanu sakulolani kuchita chotero.

Lonjezo lakuti adzabadwa mneneri womveka

15 Yehova Mulungu wanu adzakuukitsiranimneneriwa pakati panu, wa abale anu, wonga ine; muzimvera iye;

16 monga mwa zonse munafunsa Yehova Mulungu wanu mu Horebu, tsiku lakusonkhana lija, ndi kuti, Tisamvenso mau a Yehova Mulungu wathu, ndipo tisaonenso moto waukulu uwu, kuti tingafe.

17 Ndipo Yehova anati kwa ine, Chokoma ananenachi.

18 Ndidzawaukitsira mneneri wa pakati pa abale ao, wonga iwe; ndipo ndidzampatsa mau anga m’kamwa mwake, ndipo adzanena nao zonse ndimuuzazi.

19 Ndipo kudzakhala kuti munthu wosamvera mau anga amene amanena m’dzina langa, ndidzamfunsa.

20 Koma mneneri wakuchita modzikuza ndi kunena mau m’dzina langa, amene sindinamlamulire anene, kapena kunena m’dzina la milungu ina, mneneri ameneyo afe.

21 Ndipo mukati m’mtima mwanu, Tidzazindikira bwanji mau amene Yehova sananene?

22 Mneneri akanena m’dzina la Yehova, koma mau adanenawa sachitika, nisafika, ndiwo mau Yehova sanawanene; mneneriyo ananena modzikuza, musamuope iye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/18-acddb736ae7b1b77e4e4487a2c5bafbf.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 19

Za mizinda yopulumukirako

1 Pamene Yehova Mulungu wanu ataonongaamitundu, amene Yehova Mulungu wanu akupatsani dziko lao, ndipo mutalilandira lanulanu, ndi kukhala m’mizinda mwao, ndi m’nyumba zao;

2 pamenepo mudzipatulire mizinda itatu pakati padziko lanu, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanulanu.

3 Mudzikonzere njira, ndi kugawa malire a dziko lanu, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanulanu, patatu; kuti wakupha munthu athawireko.

4 Ndipo mlandu wa munthu wakupha mnzake wakuthawirako nakhala ndi moyo ndiwo: wakupha mnzake osati dala, osamuda kale lonse;

5 monga ngati munthu analowa kunkhalango ndi mnzake kutema mitengo, ndi dzanja lake liyendetsa nkhwangwa kutema mtengo, ndi nkhwangwa iguluka m’mpinimo, nikomana ndi mnzake, nafa nayo; athawire ku wina wa mizinda iyi, kuti akhale ndi moyo;

6 kuti wolipsa mwazi angalondole wakupha mnzake, pokhala mtima wake watentha, nampeza, popeza njira njaitali, namkantha kuti wafa; angakhale sanapalamule imfa, poona sanamude kale lonse.

7 Chifukwa chake ndikuuzani ndi kuti, Mudzipatulire mizinda itatu.

8 Ndipo Yehova Mulungu wanu akakulitsa malire anu, monga analumbirira makolo anu, ndi kukupatsani dziko lonse limene ananena kwa makolo anu kuwapatsa ili;

9 ukadzasunga lamulo ili lonse kulichita, limene ndikuuzani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kuyenda m’njira zake masiku onse; pamenepo mudzionjezere mizinda itatu ina pamodzi ndi itatu iyi;

10 kuti angakhetse mwazi wosachimwa pakati padziko lanu, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale cholowa chanu, pangakhale mwazi pa inu.

11 Koma munthu akamuda mnzake, namlalira, ndi kumuukira ndi kumkantha moyo wake, kuti wafa; nakathawira ku wina wa mizinda iyi;

12 pamenepo akulu a mzinda wake atumize ndi kumtengako ndi kumpereka m’manja mwa wolipsa mwazi, kuti afe.

13 Diso lanu lisamchitire chifundo, koma muchotse mwazi wosachimwa mu Israele, kuti chikukomereni.

Za kusendeza malire, ndi za mboni yonama

14 Musamasendeza malire a mnansi wanu, amene adawaika iwo a kale lomwe, m’cholowa chanu mudzalandirachi, m’dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanulanu.

15 Mboni imodzi isamaukira munthu pa mphulupulu iliyonse, kapena tchimo lililonse adalichimwa; pakamwa pa mboni ziwiri, kapena pakamwa pa mboni zitatu mlandu utsimikizike.

16 Mboni yachiwawa ikaukira munthu kumneneza ndi kuti analakwa;

17 pamenepo anthu onse awiri, pakati pao pali makaniwo, aziima pamaso pa Yehova, pamaso pa ansembe ndi oweruza okhala m’masiku awa;

18 ndipo oweruza afunsitse bwino; ndipo taonani, mboniyo ikakhala mboni yonama, yomnamizira mbale wake;

19 mumchitire monga iye anayesa kumchitira mbale wake; motero muchotse choipacho pakati panu.

20 Ndipo otsalawo adzamva, nadzaopa, ndi kusachitanso monga choipacho pakati panu.

21 Ndipo diso lanu lisachite chifundo, moyo kulipa moyo, diso kulipa diso, dzino kulipa dzino, dzanja kulipa dzanja, phazi kulipa phazi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/19-dc075c082b3f9147b2b7439c3996a220.mp3?version_id=1068—