Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli likutchedwa

Deuteronomo

, ndiye kuti “Kubwereza”, chifukwa likulongosola kachiwiri zina ndi zina zimene zidakambidwa kale m’mabuku ena aja. Bukuli likulongosola za malangizo osiyanasiyana amene Mose adapereka kwa ana a Israele pamene anali m’dziko la Mowabu, ali pafupi kulowa m’dziko lamalonjezano la Kanani.

Phunziro lalikulu lopezeka m’bukuli ndi lakuti Yehova apulumutsa Aisraele ndi kuwadalitsa chifukwa amawakonda kwambiri. Motero iwonso ayenera kumakumbukira zimenezi ndi kumkonda Iyeyo potsata malamulo ake, kuti akhale ndi moyo ndi kulandirabe madalitso ena pa moyo wao ukudzawu. Mau odziwika kwambiri apezeka pa 6.4-6: “ndipo muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, ndi mphamvu yanu yonse.” Paja Yesu adati, pa malamulo onse, lamulo lalikulu ndi lomweli.

Za mkatimu

Malangizo oyamba a Mose

1.1—4.49

Malangizo achiwiri a Mose

5.1—26.19

a. Za Malamulo Khumi

5.1—10.22

b. Mose aperekanso malamulo ena ndi malangizo

11.1—26.19

Machenjezo asanalowe m’dziko la malonjezano

27.1—28.68

Yehova achita chipangano ndi anthu ake

29.1—30.20

Malangizo otsiriza a Mose

31.1—34.12

a. Mose asankha Yoswa kuti adzalowe m’malo mwake

31.1—33.29

b. Imfa ya Mose

34.1-12

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 1

Mose awafotokozera za ulendo wao m’chipululu

1 Awa ndi mau amene Mose ananena kwa Israele wonse, tsidya la Yordani m’chipululu, m’chidikha cha pandunji pa Sufu, pakati pa Parani, ndi Tofele, ndi Labani, ndi Hazeroti, ndi Dizahabu.

2 Ulendo wake wochokera ku Horebu wofikira ku Kadesi-Baranea, wodzera njira ya phiri la Seiri, ndiwo wa masiku khumi ndi limodzi.

3 Ndipo kunali, chaka cha makumi anai, mwezi wakhumi ndi umodzi, tsiku loyamba la mweziwo, Mose ananena ndi ana a Israele, monga mwa zonse Yehova adamlamulira awauze;

4 atakantha Sihoni mfumu ya Aamori, wakukhala mu Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya Basani, wakukhala mu Asitaroti, ku Ederei.

5 Tsidya lija la Yordani, m’dziko la Mowabu, Mose anayamba kufotokozera chilamulo ichi, ndi kuti,

6 Yehova Mulungu wathu ananena ndi ife mu Horebu, ndi kuti Yakwanira nthawi yokhala inu m’phiri muno;

7 bwererani, yendani ulendo wanu ndi kumuka ku mapiri a Aamori, ndi koyandikizana nao, kuchidikha, kumapiri, ndi kunsi ndi kumwera, ndi kumphepete kwa nyanja, dziko la Akanani, ndi Lebanoni, kufikira mtsinje waukulu wa Yufurate.

8 Taonani, ndakupatsani dzikoli pamaso panu, lowani landirani dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo, kuti ili ndidzawapatsa iwo ndi mbeu zao pambuyo pao.

9 Ndipo muja ndinanena ndi inu, ndi kuti, Sinditha ine kukunyamulani ndekha;

10 Yehova Mulungu wanu anakuchulukitsani, ndipo taonani, lero muchuluka ngati nyenyezi za kumwamba.

11 Yehova Mulungu wa makolo anu, achulukitsire chiwerengero chanu chalero ndi chikwi chimodzi, nakudalitseni monga Iye ananena nanu!

12 Ndikasenza bwanji ndekha kupsinya kwanu, ndi katundu wanu, ndi kulimbana kwanu?

13 Dzifunireni amuna anzeru, ndi ozindikira bwino, ndi odziwika mwa mafuko anu, ndipo ndidzawaika akhale akulu anu.

14 Pamenepo munandiyankha ndi kuti, Mau mwanenawa ndi abwino kuwachita.

15 Potero ndinatenga akulu a mafuko anu, amuna anzeru, ndi odziwika, ndi kuwaika akhale akulu anu, atsogoleri a zikwi, ndi atsogoleri a mazana, ndi atsogoleri a makumi asanu, ndi atsogoleri a makumi, ndi akapitao, a mafuko anu.

16 Ndipo ndinauza oweruza anu muja, ndi kuti, Mverani milandu ya pakati pa abale anu, ndi kuweruza kolungama pakati pa munthu ndi mbale wake, ndi mlendo wokhala naye.

17 Musamasamalira munthu poweruza mlandu; ang’ono ndi akulu muwamvere chimodzimodzi; musamaopa nkhope ya munthu; popeza chiweruzo ncha Mulungu; ndipo mlandu ukakukanikani mubwere nao kwa ine, ndidzaumva.

18 Ndipo ndinakuuzani muja zonse muyenera kuzichita.

19 Pamenepo tinayenda ulendo kuchokera ku Horebu, ndi kubzola m’chipululu chachikulu ndi choopsa chija chonse munachionachi, panjira ya ku mapiri a Aamori, monga Yehova Mulungu wathu anatiuza; ndipo tinadza ku Kadesi-Baranea.

20 Ndipo ndinati kwa inu, Mwafikira mapiri a Aamori, amene Yehova Mulungu wathu atipatsa.

21 Taonani, Yehova Mulungu wanu wapatsa dzikoli pamaso panu; kwerakoni, landirani, monga Yehova Mulungu wa makolo anu, wanena ndi inu; musamachita mantha, musamatenga nkhawa.

22 Ndipo munayandikiza kwa ine inu nonse, ndi kuti, Titumize amuna atitsogolere, kuti akatizondere dziko ndi kutibwezera mau akunena za njira ya kukwera nayo ife pomka komwemo, ndi za mizinda yoti tidzafikako.

23 Ndipo chinandikomera chinthu ichi; ndipo ndinatenga amuna khumi ndi awiri a inu, fuko limodzi mwamuna mmodzi;

24 amenewa anatembenuka nakwera kumapiri nalowa ku chigwa cha Esikolo, nachizonda.

25 Ndipo anatengako zipatso za dzikoli m’manja mwao, natsikira nazo kwa ife, natibwezera mau ndi kuti, Dzikoli Yehova Mulungu wathu atipatsa ndi labwino.

26 Koma simunafune kukwerako, ndipo munapikisana nao mau a Yehova Mulungu wanu.

27 Ndipo munadandaula m’mahema mwanu, ndi kuti, Popeza anatida Yehova, Iye anatitulutsa m’dziko la Ejipito, kutipereka m’manja mwa Aamori, ationonge.

28 Tikwere kuti? Abale athu atimyukitsa mitima yathu, ndi kuti, Anthuwo ndiwo aakulu ndi aatali akuposa ife; mizinda ndi yaikulu ndi ya malinga ofikira m’mwamba: tinaonakonso ana a Anaki.

29 Pamenepo ndinati kwa inu, Musamaopsedwa, musamachita mantha nao.

30 Yehova Mulungu wanu wakutsogolera inu, Iye adzathirira inu nkhondo, monga mwa zonse anakuchitirani mu Ejipito pamaso panu;

31 ndi kuchipululu, kumene munapenya kuti Yehova Mulungu wanu anakunyamulani, monga anyamula mwana wake wamwamuna, m’njira monse munayendamo, kufikira mutalowa m’malo muno.

32 Koma m’chinthu ichi simunakhulupirire Yehova Mulungu wanu,

33 amene anakutsogolerani m’njira, kukufunirani malo akumanga mahema anu ndi moto usiku, kukuonetserani njira yoyendamo inu, ndi mumtambo usana.

34 Ndipo Yehova anamva mau a kunena kwanu, nakwiya, nalumbira, ndi kuti,

35 Palibe mmodzi wa anthu awa a mbadwo uno woipa adzaona dziko lokomalo ndinalumbira kupatsa makolo anuli.

36 Koma Kalebe mwana wa Yefune, iye adzaliona; ndidzampatsa iye dziko limene anapondapo, ndi ana ake; popeza analimbika ndi kutsata Yehova.

37 Yehova anakwiya ndi inenso chifukwa cha inu, ndi kuti, Iwenso sudzalowamo.

38 Yoswa mwana wa Nuni, wakuima pamaso pako, iye adzalowamo; umlimbitse mtima; popeza iye adzalandiritsa Israele.

39 Ndipo ana anu amene mudanena, Adzakhala ogulidwa, ndi ana anu osadziwa chabwino kapena choipa ndi pano, iwo adzalowamo, ndidzawapatsa iwo ili, adzalilandira ndi iwo.

40 Koma inu, bwererani, mukani ulendo wanu kuchipululu, njira ya ku Nyanja Yofiira.

41 Pamenepo munayankha ndi kunena ndi ine, Tachimwira Yehova, tidzakwera ndi kuthira nkhondo monga mwa zonse Yehova Mulungu wathu atiuza. Ndipo munadzimangira munthu yense zida zake za nkhondo, nimunakonzeka kukwera kunka kumapiri.

42 Koma Yehova anati kwa ine, Nena nao, Musakwerako, kapena kuthira nkhondo; popeza sindili pakati panu; angakukantheni adani anu.

43 Pamene ndinanena ndi inu simunamvere; koma munatsutsana nao mau a Yehova ndi kuchita modzikuza, nimunakwera kunka kumapiri.

44 Ndipo Aamori, akukhala m’mapiri muja, anatuluka kukomana ndi inu, nakupirikitsani, monga zimachita njuchi, nakukanthani mu Seiri, kufikira ku Horoma.

45 Ndipo munabwerera ndi kulira pamaso pa Yehova; koma Yehova sanamvere mau anu, kapena kukutcherani khutu.

46 Potero munakhala mu Kadesi masiku ambiri, monga mwa masiku munakhalako.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/1-cc1ccbb8fbb00bf5a88eed87ee5245ec.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 2

1 Pamenepo tinabwerera, ndi kuyenda kunka kuchipululu, kutsata njira ya Nyanja Yofiira, monga Yehova adanena ndi ine; ndipo tinapaza phiri la Seiri masiku ambiri.

2 Ndipo Yehova ananena ndi ine, ndi kuti,

3 Yakwanira nthawi yakupaza inu phiri ili; tembenukani kunka kumpoto.

4 Ndipo uuze anthu, ndi kuti, Mukapite kubzola malire a abale anu, ana a Esau okhala mu Seiri; ndipo adzakuopani; muchenjere ndithu;

5 musalimbana nao; popeza sindikupatsakoni dziko lao, pangakhale popondapo phazi lanu ai; pakuti ndapatsa Esau phiri la Seiri likhale lakelake.

6 Mugulane nao chakudya ndi ndalama, kuti mudye; mugulane naonso madzi kuti mumwe.

7 Pakuti Yehova Mulungu wanu anakudalitsani mu ntchito zonse za manja anu; anadziwa kuyenda kwanu m’chipululu ichi chachikulu; zaka izi makumi anai Yehova Mulungu wanu anakhala ndi inu; simunasowe kanthu.

8 Potero tinapitirira abale athu, ana a Esau okhala mu Seiri, njira ya chidikha, ku Elati ndi ku Eziyoni-Gebere. Pamenepo tinatembenuka ndi kudzera njira ya chipululu cha Mowabu.

9 Ndipo Yehova anati kwa ine, Usavuta Mowabu, kapena kuutsana naye nkhondo; popeza sindidzakupatsako dziko lake likhale lakolako; pakuti ndinapatsa ana a Loti Ari likhale laolao.

10 (Aemimu anakhalamo kale, ndiwo anthu aakulu, ndi ambiri, ndi ataliatali, ngati Aanaki.

11 Anawayesa iwonso Arefaimu, monga Aanaki; koma Amowabu awatcha Aemimu.

12 Ndipo Ahori anakhala mu Seiri kale, koma ana a Esau analanda dziko lao, nawaononga pamaso pao, nakhala m’malo mwao; monga Israele anachitira dziko lakelake, limene Yehova anampatsa).

13 Ukani tsopano, olokani mtsinje wa Zeredi. Ndipo tinaoloka mtsinje wa Zeredi.

14 Ndipo masiku amene tinayenda kuchokera ku Kadesi-Baranea, kufikira tidaoloka mtsinje wa Zeredi, ndiwo zaka makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu; kufikira utatha mbadwo wonse wa amuna ankhondo m’chigono, monga Yehova adawalumbirira.

15 Komanso dzanja la Yehova linatsutsana nao, kuwaononga m’chigono, kufikira adawatha.

16 Ndipo kunali, atatha kufa amuna onse ankhondo mwa anthu,

17 Yehova ananena ndi ine, ndi kuti,

18 Lero lomwe utumphe malire a Mowabu, ndiwo Ari.

19 Ndipo pamene uyandikiza popenyana ndi ana a Amoni, usawavuta, kapena kuutsana nao; popeza sindidzakupatsako dziko la ana a Amoni likhale lakolako; popeza ndinapatsa ana a Loti ili likhale laolao.

20 (Ilinso aliyesa dziko la Arefaimu; Arefaimu anakhalamo kale; koma Aamoni awatcha Azamzumimu;

21 ndiwo anthu aakulu, ndi ambiri, ndi ataliatali, monga Aanaki; koma Yehova anawaononga pamaso pao; ndipo analanda dziko lao, nakhala m’malo mwao;

22 monga Iye anachitira ana a Esau, akukhala mu Seiri, pamene anaononga Ahori pamaso pao; ndipo analanda dziko lao, nakhala m’malo mwao kufikira lero lomwe.

23 Kunena za Aavimu akukhala m’midzi kufikira ku Gaza, Akafitori, akufuma ku Kafitori, anawaononga, nakhala m’malo mwao).

24 Uka, yenda ulendo wako, ndi kuoloka mtsinje wa Arinoni; taonani, ndapereka Sihoni mfumu ya Hesiboni, Mwamori, ndi dziko lake m’dzanja lako; yamba kulilandira, ndi kuutsana naye nkhondo.

25 Tsiku lino ndiyamba kuopsetsa nawe ndi kuchititsa mantha nawe anthu a pansi pa thambo lonse, amene adzamva mbiri yako, nadzanjenjemera, nadzawawidwa chifukwa cha iwe.

26 Ndipo ndinatuma amithenga ochokera ku chipululu cha Kedemoti kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni ndi mau a mtendere, ndi kuti,

27 Ndipitire m’dziko mwako; ndidzatsata mseu, osapatuka ine ku dzanja lamanja kapena kulamanzere,

28 Undigulitse chakudya ndi ndalama, kuti ndidye; ndi kundipatsa madzi kwa ndalama, kuti ndimwe; chokhachi ndipitire choyenda pansi;

29 monga anandichitira ana a Esau akukhala mu Seiri, ndi Amowabu akukhala mu Ari; kufikira nditaoloka Yordani kulowa dziko limene Yehova Mulungu wathu atipatsa.

30 Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanatilole kupitira kwao; popeza Yehova Mulungu wanu anaumitsa mzimu wake, nalimbitsa mtima wake, kuti ampereke m’dzanja lanu, monga lero lino.

31 Ndipo Yehova anati kwa ine, Taona, ndayamba kupereka Sihoni ndi dziko lake pamaso pako; yamba kulandira dziko lake likhale lakolako.

32 Pamenepo Sihoni anatuluka kukomana nafe, iye ndi anthu ake onse, kumenyana nafe nkhondo ku Yahazi.

33 Ndipo Yehova Mulungu wathu anampereka iye pamaso pathu; ndipo tinamkantha, iye ndi ana ake aamuna ndi anthu ake onse.

34 Ndipo muja tinalanda mizinda yake yonse; ndipo tinaononga konse mizinda yonse, amuna ndi akazi ndi ana; sitinasiyapo ndi mmodzi yense.

35 Zoweta zokha tinadzifunkhira, pamodzi ndi zofunkha za mizinda tidailanda.

36 Kuyambira ku Aroere, ndiko kumphepete kwa mtsinje wa Arinoni, ndi kumudzi wokhala kumtsinje kufikira ku Giliyadi, kunalibe mzinda wakutitalikira malinga ake; Yehova Mulungu wathu anapereka yonse pamaso pathu.

37 Ku dziko la ana a Amoni lokha simunayandikize; dera lonse la mtsinje wa Yaboki, ndi mizinda ya kumapiri, ndi kwina kulikonse Yehova Mulungu wathu anatiletsa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/2-6f4dc7a4f274178cf7e741faa217c2f5.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 3

1 Pamenepo tinatembenuka, ndi kubwera kunka njira ya ku Basani; ndipo Ogi mfumu ya Basani anatuluka kukomana nafe, kumenyana nafe nkhondo, iye ndi anthu ake onse, ku Ederei.

2 Ndipo Yehova anati kwa ine, Usamuopa; popeza ndampereka iye ndi anthu ake onse, ndi dziko lake, m’dzanja lako; umchitire monga umo unachitira Sihoni mfumu ya Aamori, amene anakhala mu Hesiboni.

3 Potero Yehova Mulungu wathu anaperekanso m’manja mwathu Ogi mfumu ya Basani, ndi anthu ake onse, ndipo tinamkantha kufikira sanamtsalire ndi mmodzi yense.

4 Ndipo muja tinalanda mizinda yake yonse; kunalibe mzinda sitinaulande m’manja mwao, mizinda makumi asanu ndi limodzi, dera lonse la Arigobu, dziko la Ogi mu Basani.

5 Yonseyi ndiyo mizinda yozinga ndi malinga aatali, zitseko, ndi mipiringidzo; pamodzi ndi midzi yambirimbiri yopanda malinga.

6 Ndipo tinaiononga konse, monga umo tinachitira Sihoni mfumu ya Hesiboni, ndi kuononga konse mizinda yonse, amuna, akazi ndi ana.

7 Koma zoweta zonse ndi zofunkha za m’mizinda, tinadzifunkhira tokha.

8 Ndipo muja tinalanda dziko m’manja mwa mafumu awiri a Aamori okhala tsidya lija la Yordani, kuyambira mtsinje wa Arinoni kufikira phiri la Heremoni;

9 (Asidoni alitcha Heremoni Sirioni, koma Aamori alitcha Seniri);

10 mizinda yonse ya kuchidikha, ndi Giliyadi lonse, ndi Basani lonse kufikira ku Saleka ndi Ederei, mizinda ya dziko la Ogi mu Basani.

11 (Pakuti Ogi mfumu ya Basani anatsala yekha wa iwo otsalira Arefaimu; taonani, kama wake ndiye kama wachitsulo; sukhala kodi mu Raba wa ana a Amoni? Utali wake mikono isanu ndi inai, kupingasa kwake mikono inai, kuyesa mkono wa munthu).

12 Ndipo dziko ili tinalilanda muja; kuyambira ku Aroere, wa ku mtsinje wa Arinoni, ndi dera lina la ku mapiri a Giliyadi, ndi mizinda yake, ndinapatsa Arubeni ndi Agadi.

13 Ndi chotsalira cha Giliyadi, ndi Basani lonse, dziko la Ogi, ndinapatsa hafu la fuko la Manase; dziko lonse la Arigobu, pamodzi ndi Basani. (Ndilo lotchedwa dziko la Arefaimu.

14 Yairi mwana wa Manase analanda dziko lonse la Arigobu, kufikira malire a Agesuri ndi Amaakati; nalitcha dzina lake, Basani Havoti-Yairi, kufikira lero lino).

15 Ndipo ndinampatsa Makiri Giliyadi.

16 Koma ndinapatsa Arubeni ndi Agadi kuyambira ku Giliyadi kufikira ku mtsinje wa Arinoni, pakati pa chigwa ndi malire ake, kufikira mtsinje wa Yaboki, ndiwo malire a ana a Amoni;

17 ndi chidikha, ndi Yordani ndi malire ake, kuyambira ku Kinereti kufikira ku Nyanja ya Araba, ndiyo Nyanja ya Mchere, patsinde pa Pisiga, kum’mawa.

18 Ndipo ndinauza inu muja, ndi kuti, Yehova Mulungu wanu wakupatsani dziko ili likhale lanulanu, muoloke, amuna onse amphamvu ovala zida zao, pamaso pa abale anu ana a Israele.

19 Koma akazi anu, ndi ana anu, ndi zoweta zanu, (ndidziwa muli nazo zoweta zambiri), zikhale m’mizinda yanu imene ndinakupatsani;

20 kufikira Yehova atapumulitsa abale anu, monga anapumulitsa inu, nalandira iwonso dziko limene Yehova Mulungu wanu awapatsa tsidya lija la Yordani; pamenepo mudzabwerera munthu yense ku cholowa chake, chimene ndinakupatsani.

21 Ndipo ndinauza Yoswa muja, ndi kuti, Maso ako anapenya zonse Yehova Mulungu wanu anawachitira mafumu awa awiri; momwemo Yehova adzachitira maufumu onse kumene muolokerako.

22 Musawaopa popeza Yehova Mulungu wanu, ndiye agwirira inu nkhondo.

23 Ndipo ndinapempha chifundo kwa Yehova nthawi yomwe ija, ndi kuti,

24 Ambuye Yehova, mwayamba Inu kuonetsera mtumiki wanu ukulu wanu, ndi dzanja lanu lamphamvu; pakuti Mulungu ndani m’mwamba kapena padziko lapansi wakuchita monga mwa ntchito zanu, ndi monga mwa mphamvu zanu?

25 Ndioloketu, ndilione dziko lokomali lili tsidya la Yordani, mapiri okoma aja, ndi Lebanoni.

26 Koma Yehova anakwiya ndi ine, chifukwa cha inu, sanandimvere ine; ndipo Yehova anati kwa ine, Chikukwanire, usaonjezenso kunena ndi Ine za chinthuchi.

27 Kwera kumwamba ku Pisiga, nukweze maso ako kumadzulo, ndi kumpoto, ndi kumwera, ndi kum’mawa, nuyang’ane ndi maso ako; popeza sudzaoloka Yordani uyo.

28 Koma langiza Yoswa, numlimbitse mtima, ndi kumkhwimitsa, pakuti adzaoloka pamaso pa anthu awa, nadzawalandiritsa dziko ulionali likhale laolao.

29 Potero tinakhala m’chigwamo pandunji pa Betepeori.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/3-dc539c885085cb44533767f127b19b5d.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 4

Mose awadandaulira amvere Malamulo a Mulungu

1 Ndipo tsopano, Israele, tamverani malemba ndi maweruzo, amene ndikuphunzitsani muwachite; kuti mukhale ndi moyo, ndi kulowa, ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akupatsani.

2 Musamaonjeza pa mau amene ndikuuzani, kapena kuchotsapo, kuti musunge malamulo a Yehova Mulungu wanu, amene ndikuuzani.

3 Maso anu anapenya chochita Yehova chifukwa cha Baala-Peori; pakuti amuna onse amene anatsata Baala-Peori, Yehova Mulungu wanu anawaononga pakati panu.

4 Koma inu amene munamamatira Yehova Mulungu wanu muli ndi moyo nonsenu lero lomwe.

5 Taonani, ndinakuphunzitsani malemba ndi maweruzo, monga Yehova Mulungu wanga anandiuza ine, kuti muzichita chotero pakati padziko limene munkako kulilandira likhale lanulanu.

6 Chifukwa chake asungeni, achiteni; pakuti ichi ndi nzeru zanu ndi chidziwitso chanu pamaso pa mitundu ya anthu akumva malemba ndi kuti, Ndithu mtundu waukulu uwu, ndiwo athu anzeru ndi akuzindikira.

7 Pakuti mtundu waukulu wa anthu ndi uti, wakukhala ndi Mulungu pafupi pao monga amakhala Yehova Mulungu wathu, pamene paliponse timaitanira Iye?

8 Ndipo mtundu waukulu wa anthu ndi uti, wakukhala nao malemba ndi maweruzo olungama, akunga chilamulo ichi chonse ndichiika pamaso panu lero lino?

9 Chokhachi, dzichenjerani nokha, ndi kusunga moyo wanu mwachangu, kuti mungaiwale zinthuzi adaziona maso anu, ndi kuti zisachoke kumtima kwanu masiku onse a moyo wanu; koma muzidziwitsa ana anu ndi zidzukulu zanu.

10 Tsikuli munaima pamaso pa Yehova Mulungu wanu mu Horebu muja Yehova anati kwa ine, Ndisonkhanitsire anthu, ndidzawamvetsa mau anga, kuti aphunzire kundiopa Ine masiku ao onse akukhala ndi moyo padziko lapansi, ndi kuti aphunzitse ana ao.

11 Ndipo munayandikiza ndi kuima patsinde paphiri; ndi phirilo linayaka moto kufikira pakati pa thambo; kunali mdima, ndi mtambo, inde mdima bii.

12 Pamenepo Yehova ananena ndi inu ali pakati pa moto; munamva kunena kwa mau, osaona maonekedwe, koma kunenako.

13 Pamenepo anakufotokozeranichipanganochake, chimene anakulamulirani kuchichita, ndiwo Mau Khumi; nawalemba pa magome awiri amiyala.

14 Ndipo Yehova anandilamulira muja ndikuphunzitseni malemba ndi maweruzo, kuti mukawachite m’dziko limene muolokerako kulilandira likhale lanulanu.

15 Potero dzichenjerani nao moyo wanu ndithu; popeza simunapenye mafanidwe konse tsikuli Yehova ananena ndi inu mu Horebu, ali pakati pa moto;

16 kuti mungadziipse, ndi kudzipangira fano losema, lakunga chifaniziro chilichonse, mafanidwe a mwamuna kapena mkazi;

17 mafanidwe a nyama iliyonse ili padziko lapansi, mafanidwe a mbalame iliyonse yamapiko yakuuluka m’mlengalenga,

18 mafanidwe a chinthu chilichonse chokwawa pansi, mafanidwe a nsomba iliyonse yokhala m’madzi pansi padziko;

19 ndi kuti mungakweze maso anu kupenya kumwamba, ndipo poona dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi, khamu lonse la kumwamba, munganyengedwe ndi kuzigwadira, ndi kuzitumikira, zimene Yehova Mulungu wanu anagawira mitundu yonse ya anthu pansi pa thambo lonse.

20 Koma Yehova anakutengani, nakutulutsani m’ng’anjo yamoto, mu Ejipito, mukhale kwa Iye anthu a cholowa chake, monga mukhala lero lino.

21 Yehova anakwiyanso nane chifukwa cha mau anu, nalumbira kuti sindidzaoloka Yordani ine, ndi kuti sindidzalowa m’dziko lokomali Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale cholowa chanu;

22 pakuti ndidzafa m’dziko muno, osaoloka Yordani; koma inu mudzaoloka, ndi kulandira dziko ili lokoma likhale lanulanu.

23 Dzichenjerani, mungaiwale chipangano cha Yehova Mulungu wanu, chimene anapangana nanu, ndi kuti mungadzipangire fano losema, chifaniziro cha kanthu kalikonse Yehova Mulungu wanu anakuletsani.

24 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye moto wonyeketsa, ndi Mulungu wansanje.

25 Mutakabala ana, ndi zidzukulu, ndipo mutakakhala nthawi yaikulu m’dzikomo, ndi kudziipsa, ndi kupanga fano losema, m’chifaniziro cha kanthu kalikonse, ndi kuchita choipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kuutsa mkwiyo wake:

26 ndiitana kumwamba ndi dziko lapansi zichite mboni pa inu lero lino, kuti mudzaonongeka msangatu kuchotsedwa ku dziko limene muolokera Yordani kulilandira likhale lanulanu; masiku anu sadzachuluka pamenepo, koma mudzaonongeka konse.

27 Ndipo Yehova adzakubalalitsani mwa mitundu ya anthu, nimudzatsala pang’ono mwaamitundu, kumene Yehova adzakutsogolerani kwao.

28 Ndipo kumeneko mudzatumikira milungu, ntchito ya manja a anthu, mtengo ndi mwala, yosapenya, kapena kumva, kapena kudya, kapena kununkhiza.

29 Koma mukafuna Yehova Mulungu wanu kumeneko, mudzampeza, ngati mumfunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.

30 Mukakhala nao msauko, zikakugwerani zonsezi, masiku otsiriza mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumvera mau ake;

31 popeza Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu wachifundo; sadzakusiyani, kapena kukuonongani, kapena kuiwala chipangano cha makolo anu chimene analumbirira iwo.

32 Pakuti, funsiranitu, masiku adapitawo, musanakhale inu, kuyambira tsikuli Mulungu analenga munthu padziko lapansi, ndi kuyambira malekezero ena a thambo kufikira malekezero anzake a thambo, ngati chinthu chachikulu chonga ichi chinamveka, kapena kuchitika?

33 Kodi pali mtundu wa anthu udamva mau a mulungu wina akunena pakati pa moto, monga mudamva inu, ndi kukhala ndi moyo?

34 Kapena kodi anayesa Mulungu kumuka ndi kudzitengera mtundu mwa mtundu wina wa anthu, ndi mayesero, ndi zizindikiro, ndi zozizwa, ndi nkhondo, ndi mwa dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, ndi mwa zoopsa zazikulu, monga mwa zonse Yehova Mulungu wanu anakuchitirani mu Ejipito pamaso panu?

35 Inu munachiona ichi, kuti mudziwe kuti Yehova ndiye Mulungu; palibe wina wopanda Iye.

36 Anakumvetsani mau ake kuchokera kumwamba, kuti akuphunzitseni; ndipo padziko lapansi anakuonetsani moto wake waukulu; nimunamva mau ake pakati pa moto.

37 Ndipo popeza anakonda makolo anu, anasankha mbeu zao zakuwatsata, nakutulutsani pamaso pake ndi mphamvu yake yaikulu, mu Ejipito;

38 kupirikitsa amitundu aakulu ndi amphamvu oposa inu pamaso panu, kukulowetsani ndi kukupatsani dziko lao likhale cholowa chanu, monga lero lino.

39 Potero dziwani lero lino nimukumbukire m’mtima mwanu, kuti Yehova ndiye Mulungu, m’thambo la kumwamba ndi padziko lapansi; palibe wina.

40 Muzisunga malemba ake, ndi malamulo ake, amene ndikuuzani lero lino, kuti chikukomereni inu ndi ana anu akukutsatani, ndi kuti masiku anu achuluke padziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu kosatha.

Mizinda itatu yopulumukirako kum’mawa kwa Yordani

41 Pamenepo Mose anapatula mizinda itatu tsidya lija la Yordani lotuluka dzuwa;

42 kuti athawireko wakupha munthu, osamupha mnansi wake dala, osamkwiyira ndi kale lonse; ndi kuti, akathawira ku umodzi wa mizinda iyi, akhale ndi moyo:

43 ndiyo Bezeri, m’chipululu, m’dziko lachidikha, ndiwo wa Arubeni; ndi Ramoti mu Giliyadi, ndiwo wa Agadi; ndi Golani, mu Basani, ndiwo wa Amanase.

44 Ndipo ichi ndi chilamulo Mose anachiika pamaso pa ana a Israele;

45 izi ndi mboni, ndi malemba, ndi maweruzo, Mose anazinena kwa ana a Israele, potuluka iwo mu Ejipito;

46 tsidya lija la Yordani, m’chigwa cha pandunji pa Betepeori, m’dziko la Sihoni mfumu ya Aamori, wakukhala mu Hesiboni, amene Mose ndi ana a Israele anamkantha, potuluka iwo mu Ejipito;

47 ndipo analanda dziko lake, ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani, mafumu awiri a Aamori, akukhala tsidya lija la Yordani lotuluka dzuwa;

48 kuyambira ku Aroere, ndiwo m’mphepete mwa mtsinje wa Arinoni, kufikira phiri la Sirioni (ndilo Heremoni),

49 ndi chidikha chonse tsidya lija la Yordani kum’mawa, kufikira ku Nyanja ya Araba, pa tsinde lake la Pisiga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/4-1ffa6ea78092b5e469811c196309d9f2.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 5

Mose abwereza kuwatchulira Malamulo a Mulungu

1 Ndipo Mose anaitana Aisraele onse, nanena nao, Tamverani, Israele, malemba ndi maweruzo ndinenawa m’makutu mwanu lero, kuti muwaphunzire, ndi kusamalira kuwachita.

2 Yehova Mulungu wathu anapangana nafechipanganomu Horebu.

3 Yehova sanachite chipangano ichi ndi makolo athu, koma ndi ife, ife amene tili ndi moyo tonsefe pano lero.

4 Yehova ananena ndi inu popenyana maso m’phirimo, ali pakati pa moto,

5 (ndinalinkuima pakati pa Yehova ndi inu muja, kukulalikirani mau a Yehova; popeza munachita mantha chifukwa cha moto, osakwera m’phirimo) ndi kuti:

6 Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa m’dziko la Ejipito, m’nyumba ya ukapolo.

7 Usakhale nayo milungu ina koma Ine ndekha.

8 Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena chifaniziro chilichonse cha zinthu za m’thambo la kumwamba, kapena za m’dziko lapansi, kapena za m’madzi a pansi padziko;

9 usazipembedzere izo, usazitumikire izo; chifukwa Ine Yehova Mulungu wako ndine Mulungu wansanje, wakulanga ana chifukwa cha atate wao, kufikira mbadwo wachitatu ndi wachinai wa iwo amene akudana ndi Ine;

10 ndi kuchitira chifundo anthu zikwi, a iwo amene akondana ndi Ine nasunga malamulo anga.

11 Usatchule dzina la Yehova Mulungu wako pachabe; chifukwa Yehova sadzamuyesa iye wosachimwa amene atchula pachabe dzina lakelo.

12 Samalira tsiku laSabatalikhale lopatulika, monga Yehova Mulungu wako anakulamulira.

13 Masiku asanu ndi limodzi uzigwiritsa ntchito, ndi kuchita ntchito zako zonse;

14 koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndilo Sabata la Yehova Mulungu wako; usamagwira ntchito iliyonse, iwe, kapena mwana wako wamwamuna, kapena mwana wako wamkazi, kapena wantchito wako wamwamuna, kapena wantchito wako wamkazi, kapena ng’ombe yako, kapena bulu wako, kapena zoweta zako zilizonse, kapena mlendo wokhala m’mudzi mwako; kuti wantchito wako wamwamuna ndi wantchito wako wamkazi apumule monga iwe mwini.

15 Ndipo uzikumbukira kuti unali kapolo m’dziko la Ejipito, ndi kuti Yehova Mulungu wako anakutulutsako ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasuka; chifukwa chake Yehova Mulungu wako anakulamulira kusunga tsiku la Sabata.

16 Lemekeza atate wako ndi amai ako, monga Yehova Mulungu wako anakulamulira; kuti masiku ako achuluke, ndi kuti chikukomere, m’dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.

17 Usaphe.

18 Usachite chigololo.

19 Usabe.

20 Usamnamizire mnzako.

21 Usasirire mkazi wake wa mnzako; usakhumbe nyumba yake ya mnzako, munda wake, kapena wantchito wake wamwamuna, kapena wantchito wake wamkazi, ng’ombe yake, kapena bulu wake, kapena kanthu kalikonse ka mnzako.

22 Yehova ananena mau awa kwa msonkhano wanu wonse, m’phirimo ali pakati pa moto, pamtambo, pamdima bii, ndi mau aakulu; osaonjezapo kanthu. Ndipo anawalembera pa magome awiri amiyala, nandipatsa awa.

23 Ndipo kunali, pamene munamva liu lotuluka pakati pa mdima, potentha phiri ndi moto, munayandikiza kwa ine, ndiwo mafumu onse a mafuko anu ndi akulu anu;

24 ndipo munati, Taonani, Yehova Mulungu wathu anationetsa ulemerero wake, ndi ukulu wake, ndipo tidamva liu lake ali pakati pa moto; tapenya lero lino kuti Mulungu anena ndi munthu, ndipo akhala ndi moyo.

25 Ndipo tsopano tiferenji? Popeza moto waukulu uwu udzatitha. Tikaonjeza kumva mau a Yehova Mulungu wathu, tidzafa.

26 Pakuti ndaniyo, wa zamoyo zonse adamva mau a Mulungu wamoyo wakunena ali pakati pa moto, monga ife nakhala ndi moyo?

27 Yandikizani inu, ndi kumva zonse Yehova Mulungu wathu adzati; ndipo inu munene ndi ife zonse zimene Yehova Mulungu wathu adzanena ndi inu; ndipo ife tidzazimva ndi kuzichita.

28 Ndipo Yehova anamva mau a kunena kwanu, pamene munanena ndi ine; ndipo Yehova anati kwa ine, Ndidamva mau a kunena kwao kwa anthu awa, amene ananena ndi iwe; chokoma chokhachokha adanenachi.

29 Ha? Mwenzi akadakhala nao mtima wotere wakundiopa Ine, ndi kusunga malamulo anga masiku onse, kuti chiwakomere iwo ndi ana ao nthawi zonse!

30 Muka, nuti nao, Bwererani ku mahema anu.

31 Koma iwe, uime kuno ndi Ine, ndinene ndi iwe malamulo onse, ndi malemba, ndi maweruzo, amene uziwaphunzitsa, kuti awachite m’dziko limene ndiwapatsa likhale laolao.

32 Potero muzisamalira kuchita monga Yehova Mulungu wanu anakulamulirani; musamapatuka kulamanzere kapena kulamanja.

33 Muziyenda m’njira yonse imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani, kuti mukakhale ndi moyo, ndi kuti chikukomereni, ndi kuti masiku anu achuluke m’dziko limene mudzakhala nalo lanulanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/5-98abd942bd59a754061406610597f0a5.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 6

Awapempha asunge Malamulo a Mulungu kuti adale

1 Ndipo awa ndi malamulo, malemba, ndi maweruzo, amene Yehova Mulungu wanu analamulira kukuphunzitsani, kuti muziwachita m’dziko limene muolokerako kulilandira;

2 kuti muope Yehova Mulungu wanu, kusunga malemba ake onse ndi malamulo ake, amene ndikuuzani inu ndi ana anu, ndi zidzukulu zanu, masiku onse a moyo wanu, ndi kuti masiku anu achuluke.

3 Potero imvani, Israele, musamalire kuwachita, kuti chikukomereni ndi kuti muchuluke chichulukire, monga Yehova Mulungu wa makolo anu anena ndi inu, m’dziko moyenda mkaka ndi uchi ngati madzi.

4 Imvani, Israele; Yehova Mulungu wathu, Yehova ndiye mmodzi;

5 ndipo muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, ndi mphamvu yanu yonse.

6 Ndipo mau awa ndikuuzani lero, azikhala pamtima panu;

7 ndipo muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu, ndi kuwalankhula awa pokhala pansi m’nyumba zanu, ndi poyenda inu panjira, ndi pogona inu pansi, ndi pouka inu.

8 Ndipo muziwamanga padzanja panu ngati chizindikiro, ndipo akhale ngati chapamphumi pakati pamaso anu.

9 Ndipo muziwalembera pa mphuthu za nyumba zanu, ndi pa zipata zanu.

10 Ndipo kudzakhala, Yehova Mulungu wanu atakulowetsani m’dziko limene analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo, kuti adzakupatsani ili; mizinda yaikulu ndi yokoma, imene simunaimange;

11 ndi nyumba zodzala nazo zokoma zilizonse, zimene simunazidzaze, ndi zitsime zosema, zimene simunaziseme, minda yampesa, ndi minda yaazitona, zimene simunazioke, ndipo mutakadya ndi kukhuta;

12 pamenepo mudzichenjera mungaiwale Yehova, amene anakutulutsani m’dziko la Ejipito, m’nyumba ya ukapolo.

13 Muziopa Yehova Mulungu wanu; ndi kutumikira Iyeyu; ndipo polumbira muzitchula dzina lake.

14 Musamatsate milungu ina, milungu ina ya mitundu ya anthu akuzinga inu;

15 pakuti Yehova Mulungu wanu ali pakati panu, ndiye Mulungu wansanje; kuti ungapse mtima wa Yehova Mulungu wanu, ndi kukuonongani, kukuchotsani pankhope padziko lapansi.

16 Musamayesa Yehova Mulungu wanu, monga munamyesa mu Masa.

17 Muzisunga mwachangu malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi mboni zake, ndi malemba ake, amene anakulamulirani.

18 Ndipo muzichita zolunjika ndi zokoma pamaso pa Yehova; kuti chikukomereni, ndi kuti mulowe kukalandira dziko lokomali Yehova analumbirira makolo anu,

19 kuingitsa adani anu onse pamaso panu, monga Yehova adanena.

20 Akakufunsani ana anu m’tsogolomo, ndi kuti, Mbonizo, ndi malemba, ndi maweruzo, zimene Yehova Mulungu wathu anakulamulirani, zitani?

21 Pamenepo muzinena kwa ana anu, Tinali akapolo aFaraomu Ejipito; ndipo Yehova anatitulutsa mu Ejipito ndi dzanja lamphamvu.

22 Ndipo Yehova anapatsa zizindikiro ndi zozizwa zazikulu ndi zowawa mu Ejipito, pa Farao, ndi pa nyumba yake yonse, pamaso pathu;

23 ndipo anatitulutsa komweko, kuti atilowetse, kutipatsa dzikoli analumbirira makolo athu.

24 Ndipo Yehova anatilamulira tizichita malemba awa onse, kuopa Yehova Mulungu wathu, kuti tipindule nako masiku onse, kuti atisunge amoyo, monga lero lino.

25 Ndipo kudzakhala kwa ife chilungamo, ngati tisamalira kuchita malamulo awa onse pamaso pa Yehova Mulungu wathu, monga anatilamulira ife.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/6-d790dfb15b79abb09bf31e16b28f9f46.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 7

Awapangira za Akanani ndi zipembedzo zao

1 Pamene Yehova Mulungu wanu atakulowetsani m’dziko limene munkako kulilandira likhale lanulanu, ndipo atakatayaamitunduambiri pamaso panu, Ahiti, ndi Agirigasi, ndi Aamori, ndi Akanani, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi, mitundu isanu ndi iwiri yaikulu ndi yamphamvu yoposa inu;

2 nakawapereka Yehova Mulungu wanu pamaso panu, ndipo mukawakanthe; pamenepo muwaononge konse; musapangana nao pangano, kapena kuwachitira chifundo.

3 Ndipo musakwatitsane nao; musampatse mwana wake wamwamuna mwana wanu wamkazi, kapena kutenga mwana wake wamkazi akhale wa mwana wanu wamwamuna.

4 Popeza adzapatutsa mwana wanu aleke kunditsata Ine, kuti atumikire milungu ina; potero Yehova adzapsa mtima pa inu, ndipo adzakuonongani msanga.

5 Koma muzichita nao motero: mukapasule maguwa ao a nsembe, ndi kuphwanya zoimiritsa zao, ndi kulikha zifanizo zao, ndi kutentha mafano ao osema ndi moto.

6 Pakuti inu ndinu mtundu wa anthu wopatulika wa Yehova Mulungu wanu; Yehova Mulungu wanu anakusankhani, mukhale mtundu wa pa wokha wa Iye yekha, mwa mitundu yonse ya anthu akukhala pa nkhope ya dziko.

7 Yehova sanakondwere nanu, ndi kukusankhani chifukwa cha kuchuluka kwanu koposa mitundu ina yonse ya anthu, kapena kuchepera kwanu;

8 koma Yehova anakutulutsani ndi dzanja lamphamvu, ndi kukuombolani m’nyumba ya ukapolo, m’dzanja laFaraomfumu ya Aejipito, chifukwa Yehova akukondani, ndi chifukwa cha kusunga lumbiro lija analumbirira makolo anu.

9 Chifukwa chake dziwani kuti Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu; ndiye Mulungu wokhulupirika, wakusungachipanganondi chifundo ndi iwo akumkonda ndi kusunga malamulo ake, kufikira mibadwo zikwi.

10 Ndipo awabwezera onse akudana ndi Iye, pamaso pao, kuwaononga; sachedwa naye wakudana ndi Iye, ambwezera pamaso pake.

11 Potero muzisunga malamulo, ndi malemba, ndi maweruzo amene ndikuuzani lero kuwachita.

12 Ndipo kudzakhala, chifukwa cha kumvera inu maweruzo awa, ndi kuwasunga, ndi kuwachita, Yehova Mulungu wanu adzakusungirani chipangano ndi chifundo chimene analumbirira makolo anu;

13 ndipo adzakukondani, ndi kukudalitsani, ndi kukuchulukitsani; adzadalitsanso zipatso za thupi lanu, ndi zipatso za nthaka yanu, tirigu wanu, ndi vinyo wanu, ndi mafuta anu, zoswana za ng’ombe zanu, ndi anaankhosa anu, m’dziko limene analumbirira makolo anu kuti adzakupatsani.

14 Mudzakhala odalitsika koposa mitundu yonse ya anthu; sipadzakhala mwamuna kapena wamkazi wosabala pakati pa inu, kapena pakati pa zoweta zanu.

15 Ndipo Yehova adzakuchotserani nthenda zonse; sadzakuikirani nthenda zoipa zilizonse za Aejipito muzidziwa zija; koma adzaziika pa onse akudana ndi inu.

16 Ndipo mudzatha mitundu yonse ya anthu amene Yehova Mulungu wanu adzapereka kwa inu; diso lanu lisawachitire chifundo; musamatumikira milungu yao; pakuti uku kudzakuchitirani msampha.

17 Mukadzanena m’mtima mwanu, Amitundu awa andichulukira; ndikhoza bwanji kuwapirikitsa?

18 Musamawaopa; mukumbukire bwino chimene Yehova Mulungu wanu anachitira Farao, ndi Ejipito wonse;

19 mayesero aakulu maso anu anawapenya, ndi zizindikiro, ndi zozizwa, ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, zimene Yehova Mulungu wanu anakutulutsani nazo; Yehova Mulungu wanu adzatero nayo mitundu yonse ya anthu imene muwaopa.

20 Komanso Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pao, kufikira ataonongeka otsalawo, ndi akubisala pamaso panu.

21 Musamaopa pamaso pao; popeza Yehova Mulungu wanu ali pakati pa inu, Mulungu wamkulu ndi woopsa.

22 Ndipo Yehova Mulungu wanu adzataya amitundu awa pang’onopang’ono; simuyenera kuwaononga msanga, kuti zingakuchulukireni zilombo.

23 Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka pamaso panu, nadzawapirikitsa ndi kupirikitsa kwakukulu, kufikira ataonongeka.

24 Adzaperekanso mafumu ao m’dzanja mwanu, ndipo muwafafanize maina ao pansi pa thambo; palibe munthu mmodzi adzaima pamaso panu, kufikira mutawaononga.

25 Mafano osema a milungu yao muwatenthe ndi moto; musamasirirasilivandi golide zili pa iwo, kapena kudzitengera izi; mungakodwe nazo; pakuti izi zinyansira Yehova Mulungu wanu.

26 Musamalowa nacho chonyansachi m’nyumba mwanu, kuti mungaonongeke konse pamodzi nacho; muziipidwa nacho konse, ndi kunyansidwa nacho konse; popeza ndi chinthu choyenera kuonongeka konse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/7-1a62e5a353fb959c52196993a45b2adb.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 8

Akumbuke zokoma zazikulu Mulungu anawachitira

1 Muzisamalira kuchita malamulo onse amene ndikuuzani lero lino, kuti mukhale ndi moyo, ndi kuchuluka, ndi kulowa, ndi kulandira dziko limene Yehova analumbirira makolo anu.

2 Ndipo mukumbukire njira yonse imene Yehova Mulungu wanu anakuyendetsani m’chipululu zaka izi makumi anai, kuti akuchepetseni, kukuyesani, kudziwa chokhala mumtima mwanu, ngati mudzasunga malamulo ake, kapena iai.

3 Ndipo anakuchepetsani, nakumvetsani njala, nakudyetsani ndimana, amene simunawadziwe, angakhale makolo anu sanawadziwe; kuti akudziwitseni kuti munthu sakhala wamoyo ndi mkate wokha, koma munthu akhala wamoyo ndi zonse zakutuluka m’kamwa mwa Yehova.

4 Zovala zanu sizinathe pathupi panu, phazi lanu silinatupe zaka izi makumi anai.

5 Ndipo muzindikire m’mtima mwanu, kuti monga munthu alanga mwana wake, momwemo Yehova Mulungu wanu akulangani inu.

6 Ndipo muzisunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda m’njira zake, ndi kumuopa.

7 Pakuti Yehova Mulungu wanu akulowetsani m’dziko lokoma, dziko la mitsinje yamadzi, la akasupe ndi la maiwe akutuluka m’zigwa, ndi m’mapiri;

8 dziko la tirigu ndi barele, ndi mipesa, ndi mikuyu, ndi makangaza; dziko la azitona a mafuta, ndi uchi;

9 dziko loti mudzadyamo mkate wosapereweza; simudzasowamo kanthu; dziko loti miyala yake nja chitsulo, ndi m’mapiri ake mukumbe mkuwa.

10 Ndipo mudzadya ndi kukhuta, ndi kuyamika Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko lokomali anakupatsani.

11 Chenjerani mungaiwale Yehova Mulungu wanu, ndi kusasunga malamulo ake, ndi maweruzo ake, ndi malemba ake, amene ndikuuzani lero lino;

12 kuti, mutadya ndi kukhuta, ndi kumanga nyumba zokoma, ndi kukhalamo;

13 ndipo zitachuluka ng’ombe zanu, ndi nkhosa zanu, atachulukansosilivawanu ndi golide wanu, zitachulukanso zonse muli nazo;

14 mtima wanu ungatukumuke, nimungaiwale Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani m’dziko la Ejipito, m’nyumba ya ukapolo;

15 amene anakutsogolerani m’chipululu chachikulu ndi choopsacho, munali njoka zamoto, ndi zinkhanira, mouma mopanda madzi; amene anakutulutsirani madzi m’thanthwe lansangalabwi;

16 amene anakudyetsani m’chipululu ndi mana, amene makolo anu sanawadziwe; kuti akuchepetseni, ndi kuti akuyeseni, kuti akuchitireni chokoma potsiriza panu;

17 ndipo munganene m’mtima mwanu, Mphamvu yanga ndi mkono wanga wolimba zinandifunira chuma ichi.

18 Koma mukumbukire Yehova Mulungu wanu, popeza ndi Iyeyu wakupatsani mphamvu yakuonera chuma; kuti akhazikitsechipanganochake chimene analumbirira makolo anu, monga chikhala lero lino.

19 Ndipo kudzakhala kuti mukaiwalatu Yehova Mulungu wanu, ndi kutsata milungu ina ndi kuitumikira, ndikuchitirani mboni lero lino kuti mudzaonongeka ndithu.

20 Mongaamitunduamene Yehova awaononga pamaso panu, momwemo mudzaonongeka; chifukwa cha kusamvera mau a Yehova Mulungu wanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/8-54122929546aa90c150717b099aaf210.mp3?version_id=1068—

Categories
DEUTERONOMO

DEUTERONOMO 9

1 Imvani Israele; mulikuoloka Yordani lero lino, kulowa ndi kulandiraamitunduakulu ndi amphamvu akuposa inu, mizinda yaikulu ndi ya malinga ofikira kuthambo,

2 anthu aakulu ndi ataliatali, ana a Aanaki, amene muwadziwa, amene munamva mbiri yao, ndi kuti, Adzaima ndani pamaso pa ana a Anaki?

3 Potero mudziwe lero lino, kuti Yehova Mulungu wanu ndiye amene aoloka pamaso panu ngati moto wonyeketsa; Iye adzawaononga, Iye adzawagwetsa pamaso panu; potero mudzawapirikitsa, ndi kuwaononga msanga, monga Yehova analankhula ndi inu.

4 Musamanena mumtima mwanu, atawapirikitsa pamaso panu Yehova Mulungu wanu, ndi kuti, Chifukwa cha chilungamo changa Yehova anandilowetsa kudzalandira dziko ili; pakuti Yehova awapirikitsa pamaso panu chifukwa cha zoipa za amitundu awa.

5 Simulowa kulandira dziko lao chifukwa cha chilungamo chanu, kapena mtima wanu woongoka; koma Yehova Mulungu wanu awapirikitsa pamaso panu chifukwa cha zoipa za amitundu awa, ndi kuti akhazikitse mau amene Yehova analumbirira makolo anu, Abrahamu, ndi Isaki, ndi Yakobo.

6 Potero mudziwe, kuti Yehova Mulungu wanu sakupatsani dziko ili lokoma mulilandire, chifukwa cha chilungamo chanu; pakuti inu ndinu mtundu wa anthu opulukira.

7 Kumbukirani, musamaiwala, kuti munakwiyitsa Yehova Mulungu wanu m’chipululu; kuyambira tsikuli munatuluka m’dziko la Ejipito, kufikira munalowa m’malo muno munapikisana ndi Yehova.

8 Mu Horebu momwe munautsa mkwiyo wa Yehova; ndipo Yehova anakwiya nanu kukuonongani.

9 Muja ndinakwera m’phiri kukalandira magome amiyala, ndiwo magome achipanganochimene Yehova anapangana ndi inu, ndinakhala m’phiri masiku makumi anai usana ndi usiku; osadya mkate osamwa madzi.

10 Ndipo Yehova anapereka kwa ine magome awiri amiyala, olembedwa ndi chala cha Mulungu; ndipo panalembedwa pamenepo monga mwa mau onse amene Yehova adanena ndi inu m’phirimo, ali pakati pa moto, tsiku lakusonkhana.

11 Ndipo kunali, atatha masiku makumi anai usana ndi usiku, kuti Yehova anandipatsa magome awiriwo amiyala, ndiwo magome a chipangano.

12 Ndipo Yehova anati kwa ine, Uka, fulumira kutsika kuno popeza anthu ako unawatulutsa mu Ejipitowa anadziipsa; anapatuka msanga m’njira ndinawalamulirayi; anadzipangira fano loyenga.

13 Yehova ananenanso ndi ine, ndi kuti, Ndapenya anthu awa, taona, awa ndi anthu opulukira;

14 undileke, ndiwaononge, ndi kufafaniza dzina lao pansi pa thambo; ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu wa anthu wamphamvu ndi waukulu woposa iwo.

15 Pamenepo ndinatembenuka ndi kutsika m’phiri, ndi phirilo linatentha ndi moto; ndi magome awiri a chipangano anali m’manja mwanga.

16 Ndipo ndinapenya, taonani, mudachimwira Yehova Mulungu wanu; mudadzipangira mwanawang’ombe woyenga; mudapatuka msanga m’njira imene Yehova adalamulira inu.

17 Pamenepo ndinagwira magome awiriwo, ndi kuwataya achoke m’manja anga awiri, ndi kuwaswa pamaso panu.

18 Ndipo ndinagwa pansi pamaso pa Yehova, monga poyamba paja, masiku makumi anai usana ndi usiku, osadya mkate osamwa madzi, chifukwa cha machimo anu onse mudachimwa, ndi kuchita choipacho pamaso pa Yehova, kuutsa mkwiyo wake.

19 Pakuti ndinachita mantha chifukwa cha mkwiyo waukali, umene Yehova anakwiya nao pa inu kukuonongani. Koma Yehova anandimvera nthawi ijanso.

20 Ndipo Yehova anakwiya kwambiri ndi Aroni kumuononga; koma ndinampempherera Aroni nthawi yomweyo.

21 Ndipo ndinatenga tchimo lanu, mwanawang’ombe mudampangayo, ndi mumtentha ndi moto, ndi kumphwanya, ndi kumpera bwino kufikira atasalala ngati fumbi; ndipo ndinataya fumbi lake m’mtsinje wotsika m’phirimo.

22 Ku Tabera, ndi ku Masa, ndi ku Kibroti-Hatava, munautsanso mkwiyo wa Yehova.

23 Ndipo pamene Yehova anakutumizani kuchokera ku Kadesi-Baranea, ndi kuti Kwerani, landirani dziko limene ndakupatsani; munapikisana nao mau a Yehova Mulungu wanu, osamkhulupirira, kapena kumvera mau ake.

24 Munakhala opikisana ndi Yehova kuyambira tsikuli ndinakudziwani.

25 Ndipo ndinagwa pansi pamaso pa Yehova masiku makumi anai usana ndi usiku ndinagwa pansiwa; popeza Yehova adati kuti adzakuonongani.

26 Ndipo ndinapemphera kwa Yehova ndi kuti, Yehova Mulungu, musaononga anthu anu ndi cholowa chanu, amene mudawaombola mwa ukulu wanu, amene munawatulutsa mu Ejipito ndi dzanja lamphamvu.

27 Kumbukirani atumiki anu, Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo; musapenyerera kupulukira kwa anthu awa, kapena choipa chao, kapena tchimo lao;

28 kuti linganene dziko limene mudatitulutsako, Popeza Yehova sanakhoze kuwalowetsa m’dziko limene adanena nao, ndi popeza anadana nao, anawatulutsa kuti awaphe m’chipululu.

29 Koma iwo ndiwo anthu anu ndi cholowa chanu, amene mudawatulutsa ndi mphamvu yanu yaikulu ndi dzanja lanu lotambasuka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/DEU/9-b65d91be500dab45c0b8d5c3a6b0d6a0.mp3?version_id=1068—