Categories
AROMA

AROMA 10

Ayuda anataya chilungamo cha Mulungu

1 Abale, kufunitsa kwa mtima wanga ndi pemphero langa limene ndiwapempherera kwa Mulungu, ndilo, kuti apulumuke.

2 Pakuti ndiwachitira iwo umboni kuti ali ndi changu cha kwa Mulungu, koma si monga mwa chidziwitso.

3 Pakuti pakusadziwa chilungamo cha Mulungu, ndipo pofuna kukhazikitsa chilungamo cha iwo okha, iwo sanagonje ku chilungamo cha Mulungu.

4 PakutiKhristuali chimaliziro cha lamulo kulinga kuchilungamo kwa aliyense amene akhulupirira.

5 Pakuti Mose walemba kuti munthu amene achita chilungamo cha m’lamulo, adzakhala nacho ndi moyo.

6 Koma chilungamo cha chikhulupiriro chitero, Usamanena mumtima mwako, Adzakwera ndani Kumwambako? Ndiko, kutsitsako Khristu;

7 kapena, Adzatsikira ndani ku chiphompho chakuya? Ndiko, kukweza Khristu kwa akufa,

8 Koma chitani? Mau ali pafupi ndiwe, m’kamwa mwako, ndi mumtima mwako; ndiwo mau a chikhulupiriro, amene ife tiwalalikira:

9 kuti ngati udzavomereza m’kamwa mwako Yesu ndiye Ambuye, ndi kukhulupirira mumtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka:

10 pakuti ndi mtima munthu akhulupirira kutengapo chilungamo; ndi m’kamwa avomereza kutengapo chipulumutso.

11 Pakuti lembo litere, Amene aliyense akhulupirira Iye, sadzachita manyazi.

12 Pakuti kulibe kusiyana Myuda ndi Mgriki; pakuti Yemweyo ali Ambuye wa onse, nawachitira zolemera onse amene aitana pa Iye;

13 pakuti, aliyense amene adzaitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.

14 Ndipo iwo adzaitana bwanji pa Iye amene sanamkhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji Iye amene sanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji wopanda wolalikira?

15 Ndipo adzalalikira bwanji, ngati satumidwa? Monganso kwalembedwa, Okometsetsa ndithu ali mapazi a iwo akulalikira Uthenga Wabwino wa zinthu zabwino.

16 Koma sanamvere Uthenga Wabwino onsewo. Pakuti Yesaya anena, Ambuye, anakhulupirira ndani zonena ife?

17 Chomwecho chikhulupiriro chidza ndi mbiri, ndi mbiri idza mwa mau a Khristu.

18 Koma ine nditi, Sanamva iwo kodi! Indetu,

Liu lao linatulukira kudziko lonse lapansi,

ndi maneno ao ku malekezero a dziko lokhalamo anthu.

19 Koma nditi, Kodi Israele alibe kudziwa? Poyamba Mose anena,

Ine ndidzachititsa inu nsanje ndi iwo

amene sakhala mtundu wa anthu,

ndidzakwiyitsa inu ndi mtundu wopulukira.

20 Ndipo Yesaya alimbika mtima ndithu, nati,

Ndinapezedwa ndi iwo amene sanandifune;

ndinaonekera kwa iwo amene sanandifunse.

21 Koma kwa Israele anena, Dzuwa lonse ndinatambalitsira manja anga kwa anthu osamvera ndi okanakana.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ROM/10-314b137f34fede060bc9942c7fb5e0f2.mp3?version_id=1068—

Categories
AROMA

AROMA 11

Mulungu sanataye Aisraele onse

1 Chifukwa chake ndinena, Mulungu anataya anthu ake kodi? Msatero ai. Pakuti inenso ndili Mwisraele, wa mbeu ya Abrahamu, wa fuko la Benjamini.

2 Mulungu sanataye anthu ake amene Iye anawadziwiratu. Kapena simudziwa kodi chimene lembo linena za Eliya? Kuti anaumirira Mulungu poneneza Israele, kuti,

3 Ambuye, anawapha aneneri anu, nagwetsa maguwa anu a nsembe; ndipo ine ndatsala ndekha, ndipo alikufuna moyo wanga.

4 Koma kuyankha kwa Mulungu kudatani kwa iye? Ndinadzisiyira ndekha anthu aamuna zikwi zisanu ndi ziwiri, amene sanagwadireBaala.

5 Choteronso nthawi yatsopano chilipo chotsalira monga mwa kusankha kwa chisomo.

6 Koma ngati kuli ndi chisomo, sikulinso ndi ntchito ai; ndipo pakapanda kutero, chisomo sichikhalanso chisomo.

7 Ndipo chiyani tsono? Ichi chimene Israele afunafuna sanachipeze; koma osankhidwawo anachipeza, ndipo otsalawo anaumitsidwa mtima;

8 monga kunalembedwa kuti, Mulungu anawapatsa mzimu watulo, maso kuti asapenye, ndi makutu kuti asamve, kufikira lero lino.

9 Ndipo Davide akuti,

Gome lao likhale kwa iwo, ngati msampha, ndi ngati diwa,

ndi monga chokhumudwitsa, ndi chowabwezera chilango;

10 maso ao adetsedwe, kuti asapenye,

ndipo muweramitse msana wao masiku onse.

11 Chifukwa chake ndinena, Anakhumudwa kodi kuti agwe? Msatero ai; koma ndi kulakwa kwao chipulumutso chinadza kwa anthu akunja, kudzachititsa iwo nsanje.

12 Ndipo ngati kulakwa kwao, kwatengera dziko lapansi zolemera, ndipo kuchepa kwao kutengera anthuamitunduzolemera; koposa kotani nanga kudzaza kwao?

Potsiriza Mulungu adzapulumutsa Israele

13 Koma ndilankhula ndi inu anthu amitundu. Popeza ine ndilimtumwiwa anthu amitundu, ndilemekeza utumiki wanga;

14 kuti ngati nkutheka ndikachititse nsanje anthu a mtundu wanga, ndi kupulumutsa ena a iwo.

15 Pakuti ngati kuwataya kwao kuli kuyanjanitsa kwa dziko lapansi, nanga kulandiridwa kwao kudzatani, koma ndithu ngati moyo wakuchokera kwa akufa?

16 Ndipo ngati zipatso zoyamba zili zopatulika, choteronso mtanda; ndipo ngati muzu uli wopatulika, choteronso nthambi.

17 Koma ngati nthambi zina zinathyoledwa, ndipo iwe, ndiwe mtengo wa azitona wakuthengo, unalumikizidwa mwa izo, nugawana nazo za muzu za mafuta ake a mtengowo,

18 usadzitama iwe wekha pa nthambizo: koma ngati udzitama wekha, suli iwe amene unyamula muzu, ai, koma muzu ukunyamula iwetu.

19 Ndipo kapena udzanena, Nthambizo zathyoledwa kuti ine ndikalumikizidwe nao.

20 Chabwino; iwo anathyoledwa ndi kusakhulupirira kwao, ndipo iwe umaima ndi chikhulupiriro chako. Usamadzikuza mumtima, koma opatu:

21 pakuti ngati Mulungu sanaleke nthambi za mtundu wake, inde sadzakuleka iwe.

22 Chifukwa chake onani kukoma mtima ndi kuuma mtima kwake kwa Mulungu: kwa iwo adagwa, kuuma kwake; koma kwa iwe kukoma mtima kwake kwa Mulungu, ngati ukhala chikhalire m’kukoma mtimamo; koma ngati sutero, adzakusadza iwe.

23 Ndipo iwonso, ngati sakhala chikhalire mu kusakhulupirira, adzawalumikizanso, pakuti Mulungu ali wamphamvu yakutha kuwalumikizanso.

24 Pakuti ngati iwe unasadzidwa kumtengo waazitonawa mtundu wakuthengo, ndipo unalumikizidwa ndi mtengo wa azitona wabwino, mokaniza makhalidwe ako; koposa kotani nanga iwo, ndiwo nthambi za mtundu wake, adzalumikizidwa ndi mtengo wao womwewo wa azitona?

25 Pakuti sindifuna, abale, kuti mukhale osadziwa chinsinsi ichi, kuti mungadziyese anzeru mwa inu nokha, kuti kuuma mtima kunadza pang’ono pa Israele, kufikira kudzaza kwa anthu amitundu kunalowa;

26 ndipo chotero Israele yense adzapulumuka; monganso kunalembedwa, kuti,

Adzatuluka kuZiyoniMpulumutsi;

Iye adzachotsa zamwano kwa Yakobo:

27 Ndipo ichi ndichipanganochanga ndi iwo,

pamene ndidzachotsa machimo ao.

28 Kunena za Uthenga Wabwino, iwo ali ngati adani, chifukwa cha inu; koma kunena za chisankhidwe, ali okondedwa, chifukwa cha makolo.

29 Pakuti mphatso zake ndi kuitana kwake kwa Mulungu sizilapika.

30 Pakuti monga inunso kale simunamvere Mulungu, koma tsopano mwalandira chifundo mwa kusamvera kwao,

31 choteronso iwo sanamvere tsopano, kuti iwonso akalandire chifundo, chifukwa cha chifundo cha kwa inu.

32 Pakuti Mulungu anatsekera pamodzi onse m’kusamvera, kuti akachitire onse chifundo.

Ulemu waukulu wa Mulungu

33 Ha! Kuya kwake kwa kulemera ndi kwa nzeru ndi kwa kudziwa kwake kwa Mulungu! Osasanthulikadi maweruzo ake, ndi njira zake nzosalondoleka!

34 Pakuti anadziwitsa ndani mtima wake wa Ambuye? Kapena anakhala phungu wake ndani?

35 Ndipo anayamba ndani kumpatsa Iye, ndipo adzambwezeranso?

36 Chifukwa zinthu zonse zichokera kwa Iye, zichitika mwa Iye, ndi kufikira kwa Iye. Kwa Iyeyo ukhale ulemerero kunthawi zonse.Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ROM/11-0366ed0e0c9b4e03dada5fbc2df45978.mp3?version_id=1068—

Categories
AROMA

AROMA 12

Kudzipereka nsembe kwa Mulungu

1 Chifukwa chake ndikupemphani inu, abale, mwa zifundo za Mulungu, kuti mupereke matupi anu nsembe yamoyo, yopatulika, yokondweretsa Mulungu, ndiko kupembedza kwanu koyenera.

2 Ndipo musafanizidwe ndi makhalidwe a pansi pano: koma mukhale osandulika, mwa kukonzanso kwa mtima wanu, kuti mukazindikire chimene chili chifuniro cha Mulungu, chabwino, ndi chokondweretsa, ndi changwiro.

3 Pakuti ndi chisomo chapatsidwa kwa ine, ndiuza munthu aliyense wa inu, kuti asadziyese koposa kumene ayenera kudziyesa; koma aganize modziletsa yekha, monga Mulungu anagawira kwa munthu aliyense muyeso wa chikhulupiriro.

4 Pakuti monga m’thupi limodzi tili nazo ziwalo zambiri, ndipo ziwalo zonsezo sizili nayo ntchito imodzimodzi;

5 chomwecho ife, ndife ambiri, tili thupi limodzi mwaKhristu, ndi ziwalo zinzake, wina ndi wina.

6 Ndipo pokhala ife ndi mphatso zosiyana, monga mwa chisomo chipatsidwa kwa ife, kapena mphatso yakunenera, tinenere monga mwa muyeso wa chikhulupiriro;

7 kapena yakutumikira, tidzipereke ku utumiki uwu; kapena iye wakuphunzitsa, kukuphunzitsako;

8 kapena iye wakudandaulira, kukudandaulirako; wakugawira achite ndi mtima woona; iye wakuweruza, aweruze ndi changu; iye wakuchita chifundo, achite ndi kukondwa mtima.

Makhalidwe okoma otiyenera

9 Chikondano chikhale chopanda chinyengo. Dana nacho choipa; gwirizana nacho chabwino.

10 M’chikondano cha anzanu wina ndi mnzake mukondane ndi chikondi chenicheni; mutsogolerane ndi kuchitira wina mnzake ulemu;

11 musakhale aulesi m’machitidwe anu; khalani achangu mumzimu, tumikirani Ambuye;

12 kondwerani m’chiyembekezo, pirirani m’masautso; limbikani chilimbikire m’kupemphera.

13 Patsani zosowa oyera mtima; cherezani aulendo.

14 Dalitsani iwo akuzunza inu; dalitsani, musawatemberere.

15 Kondwani nao iwo akukondwera; lirani nao akulira.

16 Mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake. Musasamalire zinthu zazikulu, koma phatikanani nao odzichepetsa. Musadziyesere anzeru mwa inu nokha.

17 Musabwezere munthu aliyense choipa chosinthana ndi choipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pamaso pa anthu onse.

18 Ngati nkutheka, monga momwe mukhoza, khalani ndi mtendere ndi anthu onse.

19 Musabwezere choipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.

20 Koma ngati mdani wako akumva njala, umdyetse, ngati akumva ludzu, ummwetse; pakuti pakutero udzaunjika makala a moto pamutu pake.

21 Musagonje kwa choipa, koma ndi chabwino gonjetsani choipa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ROM/12-83b447fa434c854ad54ea73de6ff5fdf.mp3?version_id=1068—

Categories
AROMA

AROMA 13

Kugonjera kwathu kwa akulu

1 Anthu onse amvere maulamuliro a akulu; pakuti palibe ulamuliro wina koma wochokera kwa Mulungu; ndipo iwo amene alipo aikidwa ndi Mulungu.

2 Kotero kuti iye amene atsutsana nao ulamuliro, akaniza choikika ndi Mulungu; ndipo iwo akukaniza, adzadzitengera kulanga.

3 Pakuti mafumu sakhala oopsa ntchito zabwino koma zoipa. Ndipo ufuna kodi kusaopa ulamuliro? Chita chabwino, ndipo udzalandira kutama m’menemo:

4 pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu, kuchitira iwe zabwino. Koma ngati uchita choipa, opatu, pakuti iye sagwira lupanga kwachabe; pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu wakukwiyira ndi kubwezera chilango wochita zoipa.

5 Chifukwa chake, kuyenera kuti mukhale omvera, si chifukwa cha mkwiyo wokha, komanso chifukwa cha chikumbumtima.

6 Pakuti chifukwa cha ichi mupatsanso msonkho; pakuti iwo ndiwo atumiki a Mulungu akulabadirabe chinthu chimenechi.

7 Perekani kwa anthu onse mangawa ao; msonkho kwa eni ake a msonkho; kulipira kwa eni ake a kulipidwa; kuopa kwa eni ake a kuwaopa; ulemu kwa eni ake a ulemu.

Kukondana, kudikira, chiyero

8 Musakhale ndi mangawa kwa munthu aliyense, koma kukondana ndiko; pakuti iye amene akondana ndi mnzake wakwanitsa lamulo.

9 Pakuti ili, Usachite chigololo, Usaphe, Usabe, Usasirire, ndipo lingakhale lamulo lina lililonse, limangika pamodzi m’mau amenewa, kuti, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe wekha.

10 Chikondano sichichitira mnzake choipa; chotero chikondanocho chili chokwanitsa lamulo.

11 Ndipo chitani ichi, podziwa inu nyengo, kuti tsopano ndiyo nthawi yabwino yakuuka kutulo; pakuti tsopano chipulumutso chathu chili pafupi koposa pamene tinayamba kukhulupirira.

12 Usiku wapita, ndi mbandakucha wayandikira; chifukwa chake tivule ntchito za mdima, ndipo tivale zida za kuunika.

13 Tiyendeyende koyenera, monga usana; si m’madyerero ndi kuledzera ai, si m’chigololo ndi chonyansa ai, si mu ndeu ndi nkhwidzi ai.

14 Koma valani inu Ambuye YesuKhristu, ndipo musaganizire za thupi kuchita zofuna zake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ROM/13-cb7d964499b126a885a96adc26075530.mp3?version_id=1068—

Categories
AROMA

AROMA 14

Chipiriro cha pa ofooka

1 Ndipo iye amene ali wofooka m’chikhulupiriro, mumlandire, koma si kuchita naye makani otsutsana ai.

2 Munthu mmodzi akhulupirira kuti adye zinthu zonse, koma wina wofooka angodya zitsamba.

3 Wakudyayo asapeputse wosadyayo; ndipo wosadyayo asaweruze wakudyayo; pakuti Mulungu wamlandira.

4 Ndani iwe wakuweruza mnyamata wa mwini wake? Iye aimirira kapena kugwa kwa mbuye wake wa mwini yekha. Ndipo adzaimiritsidwa; pakuti Ambuye ali wamphamvu kumuimiritsa.

5 Munthu wina aganizira kuti tsiku lina liposa linzake; wina aganizira kuti masiku onse alingana. Munthu aliyense akhazikike konse mumtima mwake.

6 Iye wakusamalira tsiku, alisamalira kwa Ambuye: ndipo iye wakudya, adya mwa Ambuye, pakuti ayamika Mulungu; ndipo iye wosadya, mwa Ambuye sakudya, nayamikanso Mulungu.

7 Pakuti palibe mmodzi wa ife adzikhalira ndi moyo yekha, ndipo palibe mmodzi adzifera yekha.

8 Pakuti tingakhale tili ndi moyo, tikhalira Ambuye moyo; kapena tikafa, tifera Ambuye; chifukwa chake tingakhale tili ndi moyo, kapena tikafa, tikhala ake a Ambuye.

9 Pakuti, chifukwa cha ichiKhristuadafera, nakhalanso ndi moyo, kuti Iye akakhale Ambuye wa akufa ndi wa amoyo.

10 Koma iwe uweruziranji mbale wako? Kapena iwenso upeputsiranji mbale wako? Pakuti ife tonse tidzaimirira kumpando wakuweruza wa Mulungu.

11 Pakuti kwalembedwa,

Pali moyo wanga, ati Ambuye, mabondo onse adzagwadira Ine,

ndipo malilime onse adzavomereza Mulungu.

12 Chotero munthu aliyense wa ife adzadziwerengera mlandu wake kwa Mulungu.

Kusamalirana

13 Chifukwa chake tisaweruzanenso wina mnzake; koma weruzani ichi makamaka, kuti munthu asaike chokhumudwitsa panjira ya mbale wake, kapena chomphunthwitsa.

14 Ndidziwa, ndipo ndakhazikika mtima mwa Ambuye Yesu, kuti palibe chinthu chonyansa pa chokha; koma kwa ameneyo achiyesa chonyansa, kwa iye chikhala chonyansa.

15 Koma ngati iwe wachititsa mbale wako chisoni ndi chakudya, pamenepo ulibe kuyendayendanso ndi chikondano. Usamuononga ndi chakudya chako, iye amene Khristu adamfera.

16 Chifukwa chake musalole chabwino chanu achisinjirire.

17 Pakuti ufumu wa Mulungu sukhala chakudya ndi chakumwa, koma chilungamo, ndi mtendere, ndi chimwemwe mwa Mzimu Woyera.

18 Pakuti iye amene atumikira Khristu mu izi akondweretsa Mulungu, navomerezeka ndi anthu.

19 Chifukwa chake tilondole zinthu za mtendere, ndi zinthu zakulimbikitsana wina ndi mnzake.

20 Usapasule ntchito ya Mulungu chifukwa cha chakudya. Zinthu zonse zili zoyera; koma kuli koipa kwa munthu amene akudya ndi kukhumudwa.

21 Kuli kwabwino kusadya nyama, kapena kusamwa vinyo, kapena kusachita chinthu chilichonse chakukhumudwitsa mbale wako.

22 Chikhulupiriro chimene uli nacho, ukhale nacho kwa iwe wekha pamaso pa Mulungu. Wodala ndiye amene sadziweruza mwini yekha m’zinthu zomwe iye wazivomereza.

23 Koma iye amene akayikakayika pakudya, atsutsika, chifukwa akudya wopanda chikhulupiriro; ndipo chinthu chilichonse chosatuluka m’chikhulupiriro, ndicho uchimo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ROM/14-a9861516477bf718c2689bc09f6ae2e0.mp3?version_id=1068—

Categories
AROMA

AROMA 15

Khristu chitsanzo cha kusamalirana kumene

1 Ndipo ife amene tili olimba tiyenera kunyamula zofooka za opanda mphamvu, ndi kusadzikondweretsa tokha.

2 Yense wa ife akondweretse mnzake, kumchitira zabwino, zakumlimbikitsa.

3 Pakuti Khristunso sanadzikondweretse yekha; koma monga kwalembedwa, Minyozo ya iwo amene anakunyoza iwe inagwa pa Ine.

4 Pakuti zonse zinalembedwa kale zinalembedwa kutilangiza, kuti mwa chipiriro ndi chitonthozo cha malembo, tikhale ndi chiyembekezo.

5 Ndipo Mulungu wa chipiriro ndi wa chitonthozo apatse inu kuti mukhale ndi mtima umodzi wina ndi mnzake, monga mwaKhristuYesu;

6 kuti nonse pamodzi, m’kamwa mmodzi, mukalemekeze Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu.

7 Chifukwa chake mulandirane wina ndi mnzake, monganso Khristu anakulandirani inu, kukachitira Mulungu ulemerero.

8 Ndipo ndinena kuti Khristu anakhala mtumiki wamdulidwe, chifukwa cha choonadi cha Mulungu, kuti alimbikitse malonjezo opatsidwa kwa makolo,

9 ndi kuti anthu a mitundu ina akalemekeze Mulungu, chifukwa cha chifundo; monga kwalembedwa,

Chifukwa cha ichi ndidzakuvomerezani Inu

pakati pa anthuamitundu,

ndidzaimbira dzina lanu.

10 Ndiponso anena, Kondwani, amitundu inu, pamodzi ndi anthu ake.

11 Ndiponso,

Tamandani Ambuye, inu a mitundu yonse;

ndipo anthu onse amtamande.

12 Ndiponso, Yesaya ati,

Padzali muzu wa Yese,

ndi Iye amene aukira kuchita ufumu pa anthu amitundu;

Iyeyo anthu amitundu adzamuyembekezera.

13 Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m’kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera.

Utumwi wake ndi zotsimikiza mtima za Paulo

14 Koma ine ndekhanso, abale anga, nditsimikiza mtima za inu, kuti inu nokhanso muli odzala ndi ubwino, odzazidwa ndi kudziwitsa konse, ndi kukhoza kudandaulirana wina ndi mnzake.

15 Koma mwina ndaposa kukulemberani molimba mtima monga kukukumbutsaninso, chifukwa cha chisomo chapatsidwa kwa ine ndi Mulungu,

16 kuti ndikhale mtumiki wa Khristu Yesu kwa anthu amitundu, wakutumikira Uthenga Wabwino wa Mulungu, kuti kupereka kwake kwa anthu amitundu kulandirike, koyeretsedwa ndi Mzimu Woyera.

17 Chifukwa chake ndili nacho chodzitamandira cha mu Khristu Yesu ndi zinthu za kwa Mulungu.

18 Pakuti sindingathe kulimba mtima kulankhula zinthu zimene Khristu sanazichite mwa ine zakumveretsa anthu amitundu, ndi mau ndi ntchito,

19 mu mphamvu ya zizindikiro ndi zozizwitsa, mu mphamvu ya Mzimu Woyera; kotero kuti ine kuyambira kuYerusalemundi kuzungulirako kufikira ku Iliriko, ndinakwanitsa Uthenga Wabwino wa Khristu;

20 ndipo chotero ndinachiyesa chinthu chaulemu kulalikira Uthenga Wabwino, pamalopo Khristu asanatchulidwe kale, kuti ndisamange nyumba pa maziko a munthu wina.

21 Koma monga kwalembedwa,

Iwo amene uthenga wake sunawafikire, adzaona,

ndipo iwo amene sanamve, adzadziwitsa.

22 Chifukwa chakenso ndinaletsedwa kawirikawiri kudza kwa inu;

23 koma tsopano, pamene ndilibe malo m’maiko akuno, ndipo pokhala ndi kulakalaka zaka zambiri kudza kwa inu, ndidzatero,

24 pamene paliponse ndidzapita ku Spaniya. Pakuti ndiyembekeza kuonana ndi inu pa ulendo wanga, ndi kuperekezedwa ndi inu panjira panga kumeneko, ngati nditayamba kukhuta pang’ono ndi kukhala ndi inu.

25 Koma tsopano ndipita ku Yerusalemu, ndilikutumikira oyera mtima.

26 Pakuti kunakondweretsa a ku Masedoniya ndiAkayakuchereza osauka a kwa oyera mtima a ku Yerusalemu.

27 Pakuti kunakondweretsa iwo; ndiponso iwo ali amangawa ao. Pakuti ngati amitundu anagawana zinthu zao zauzimu, alinso amangawa akutumikira iwo ndi zinthu zathupi.

28 Koma pamene ndikatsiriza ichi, ndi kuwasindikizira iwo chipatso ichi, ndidzapyola kwanu kupita ku Spaniya.

29 Ndipo ndidziwa kuti pamene ndikadza kwanu, ndidzafika m’kudzaza kwake kwa chidalitso cha Khristu.

30 Ndipo ndikudandaulirani, abale, ndi Ambuye wathu Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mzimu, kuti mudzalimbike pamodzi ndi ine m’mapemphero anu kwa Mulungu chifukwa cha ine;

31 kuti ndikapulumutsidwe kwa osamvera aja a ku Yudeya; ndi kuti utumiki wanga wa ku Yerusalemu ukhale wolandiridwa bwino ndi oyera mtima;

32 kuti ndi chimwemwe ndikadze kwa inu mwa chifuniro cha Mulungu, ndi kupumula pamodzi ndi inu.

33 Ndipo Mulungu wa mtendere akhale ndi inu nonse.Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ROM/15-4aefcb275210cce6597ae577fa691dfb.mp3?version_id=1068—

Categories
AROMA

AROMA 16

Zolawirana

1 Ndipereka kwa inu Febe, mlongo wathu, ndiye mtumiki wamkazi waMpingowa Ambuye wa ku Kenkrea;

2 kuti mumlandire iye mwa Ambuye, monga kuyenera oyera mtima, ndi kuti mumthandize m’zinthu zilizonse adzazifuna kwa inu; pakuti iye yekha anali wosungira ambiri, ndi ine ndemwe.

3 Mupereke moni kwa Prisika ndi Akwila, antchito anzanga mwaKhristuYesu,

4 amene anapereka khosi lao chifukwa cha moyo wanga; amene ndiwayamika, si ine ndekha, komanso Mipingo yonse ya Ambuye ya kwa anthuamitundu;

5 ndipo mupereke moni kwa Mpingo wa Ambuye wa m’nyumba mwao. Moni kwa Epeneto wokondedwa wanga, ndiye chipatso choyamba cha Asiya cha kwa Khristu.

6 Moni kwa Maria amene anadzilemetsa ndi ntchito zambiri zothandiza inu.

7 Moni kwa Androniko ndi Yunia, anansi anga, ndi andende anzanga, amene ali omveka mwaatumwi, amenenso ananditsogolera ine mwa Khristu.

8 Moni kwa Ampiliato wokondedwa wanga mwa Ambuye.

9 Moni kwa Urbano wantchito mnzathu mwa Khristu, ndi Stakisi wokondedwa wanga.

10 Moni kwa Apelesi, wovomerezedwayo mwa Khristu. Moni iwo a kwa Aristobulo.

11 Moni kwa Herodiono, mbale wanga. Moni iwo a kwa Narkiso, amene ali mwa Ambuye.

12 Moni kwa Trifena, ndi Trifosa amene agwiritsa ntchito mwa Ambuye. Moni kwa Perisi, wokondedwayo amene anagwiritsa ntchito zambiri mwa Ambuye.

13 Moni kwa Rufu, wosankhidwayo mwa Ambuye, ndi amai wake ndi wanga.

14 Moni kwa Asinkrito, Filegoni, Heremesi, Patrobasi, Herimasi ndi abale amene ali nao.

15 Moni kwa Filologo ndi Juliya, Nereo ndi mlongo wake, ndi Olimpasi, ndi oyera mtima onse ali pamodzi nao.

16 Mupatsane moni wina ndi mnzake ndi kupsompsonana kopatulika. Mipingo yonse ya Khristu ikupatsani moni.

17 Ndipo ndikudandaulirani, abale, yang’anirani iwo akuchita zopatutsana ndi zophunthwitsa, kosalingana ndi chiphunzitsocho munachiphunzira inu; ndipo potolokani pa iwo.

18 Pakuti otere satumikira Ambuye wathu Khristu, koma mimba yao; ndipo ndi mau osalaza ndi osyasyalika asocheretsa mitima ya osalakwa.

19 Pakuti kumvera kwanu kunabuka kwa anthu onse. Chifukwa chake ndikondwera ndi inu; koma ndifuna kuti mukakhale anzeru pa zabwino, koma ozungulidwa pa zoipa.

20 Ndipo Mulungu wa mtendere adzaphwanyaSatanapansi pa mapazi anu tsopano lino.

Chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.

21 Timoteo wantchito mnzanga akupatsani moni; ndi Lusio ndi Yasoni ndi Sosipatere, abale anga.

22 Ine Tersio, ndilikulemba kalata ameneyu, ndikupereka moni mwa Ambuye.

23 Gayo, mwini nyumba wolandira ine, ndi Mpingo wonse wa Ambuye, akupereka moni. Erasto, ndiye woyang’anira mzinda, akupereka moni, ndiponso Kwarto mbaleyo.

25 Ndipo kwa Iye amene ali wamphamvu yakukhazikitsa inu monga mwa Uthenga wanga Wabwino, ndi kulalikira kwa Yesu Khristu, monga mwa vumbulutso la chinsinsi chimene chinabisika mwa nthawi zonse zosayamba,

26 koma chaonetsedwa tsopano, ndi kudziwidwa kwa anthu a mitundu yonse mwa malembo a aneneriwo, monga mwa lamulo la Mulungu wosatha, kuti amvere chikhulupiriro;

27 kwa Mulungu wanzeru yekhayo, mwa Yesu Khristu, kwa yemweyo ukhale ulemerero kunthawi zonse. Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ROM/16-84121ae5e6cb979a1fbc720370f2f7c4.mp3?version_id=1068—