Categories
AMOSI

AMOSI Mau Oyamba

Mau Oyamba

Amosi anali mneneri woyamba amene uthenga wake unalembedwa pafupifupi wonse. Ngakhale amachokera ku Yuda, iye analalikira kwa anthu a mu ufumu wa kumpoto kwa Israele m’zaka za pafupifupi 750 BC. Iyi inali nthawi imeneyo dziko linali pa mtendere, ndipo zinthu zimayenda bwino kumbali ya chuma komanso anthu amakonda kupembedza. Komabe Amosi adaona kuti odyerera chuma anali olemera okha basi, ndipo iwo amagwiritsa ntchito mphamvu zawo pofuna kupondereza osauka. Kupembedza kwao kunali kwachinyengo ndipo chitetezo sichinali monga zinthu zimaonekera. Analalikira ndi mtima wake wonse komanso mwamphamvu kuti Mulungu adzaononga dzikolo. Iye anawadandaulira kuti chilungamo chiyende “ngati mtsinje wosefuka” (5.24), ndi kuti pakutero, “kapena Yehova Mulungu wa makamu adzachitira chifundo otsala a Yosefe.” (5.15)

Za mkatimu

Chiweruzo pa maiko oyandikana ndi Israele

1.1—2.5

Chiweruzo pa Israele

2.6—6.14

Masomphenya asanu

7.1—9.15

Categories
AMOSI

AMOSI 1

Chilango cha Mulungu pa amitundu ozinga Israele

1 Mau a Amosi, amene anali mwa oweta ng’ombe a ku Tekowa, ndiwo amene anawaona za Israele masiku a Uziya mfumu ya Yuda, ndi masiku a Yerobowamu mwana wa Yowasi mfumu ya Israele, zitatsala zaka ziwiri chisanafike chivomezi.

2 Ndipo anati, Yehova adzadzuma ali muZiyoni, nadzamveketsa mau ake ali muYerusalemu; podyetsa abusa padzachita chisoni, ndi mutu wa Karimele udzauma.

3 Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Damasiko, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwake; popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira zachitsulo;

4 koma ndidzatumiza moto kunyumba ya Hazaele, ndipo udzanyeketsa nyumba zachifumu za Benihadadi.

5 Ndipo ndidzathyola mpiringidzo wa Damasiko, ndi kulikha okhala m’chigwa cha Aveni, ndi iye wogwira ndodo yachifumu mu Betedeni; ndi anthu a Aramu adzalowa ndende ku Kiri, ati Yehova.

6 Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Gaza, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwake; popeza anatenga ndende anthu onse kuwapereka kwa Edomu;

7 koma ndidzatumiza moto pa linga la Gaza, ndipo udzatha nyumba zake zachifumu;

8 ndipo ndidzalikha okhala mu Asidodi, ndi iye wogwira ndodo yachifumu mu Asikeloni; ndipo ndidzabwezera Ekeroni dzanja langa limlange; ndi Afilisti otsala adzatayika, ati Ambuye Yehova.

9 Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Tiro, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwake; popeza anapereka anthu onse kwa Edomu, osakumbukira pangano lachibale;

10 koma ndidzatumiza moto pa linga la Tiro, ndipo udzanyeketsa nyumba zake zachifumu.

11 Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Edomu, kapena zinani, sindidzabweza kulanga kwake; popeza analondola mphwake ndi lupanga, nafetsa chifundo chake chonse, ndi mkwiyo wake unang’amba ching’ambire nasunga mkwiyo wake chisungire;

12 koma ndidzatumiza moto pa Temani, udzanyeketsa nyumba zachifumu za Bozira.

13 Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za ana a Amoni, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwake; popeza anatumbula akazi ali m’pakati a Giliyadi, kuti akuze malire ao;

14 koma ndidzayatsa moto pa linga la Raba, udzanyeketsa nyumba zachifumu zake, ndi kufuula tsiku la nkhondo, ndi namondwe, tsiku la kamvulumvulu;

15 ndipo mfumu yao idzalowa kundende, iyo ndi akalonga ake pamodzi, ati Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/1-e3e1be81b1dade46fd35afdd8b965bd2.mp3?version_id=1068—

Categories
AMOSI

AMOSI 2

1 Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Mowabu, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwake; popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu asanduke njereza;

2 koma ndidzatumiza moto pa Mowabu, udzanyeketsa nyumba zachifumu za Keriyoti; ndipo Mowabu adzafa ndi phokoso, ndi kufuula, ndi mau a lipenga;

3 ndipo ndidzalikha woweruza pakati pake, ndi kupha akalonga ake onse, ati Yehova.

Chilango cha Mulungu pa Yuda ndi Israele

4 Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Yuda, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwake; popeza akaniza chilamulo cha Yehova, osasunga malemba ake; ndipo awalakwitsa mabodza ao amene makolo ao anawatsata;

5 koma ndidzatumiza moto pa Yuda, udzanyeketsa nyumba zachifumu za muYerusalemu.

6 Atero Yehova, Chifukwa cha zolakwa zitatu za Israele, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwake; popeza agulitsa wolungama ndi ndalama, ndi wosowa chifukwa cha nsapato;

7 ndiwo amene aliralira fumbi lapansi lili pamutu pa wosauka, napotoza njira ya wofatsa; ndipo munthu ndi atate wake amuka kwa namwali yemweyo, kuti aipse dzina langa loyera;

8 nagona pansi pa zofunda za chikole kumaguwa a nsembe ali onse, ndi m’nyumba ya Mulungu wao akumwa vinyo wa iwo olipitsidwa.

9 Koma ndinaononga Ine pamaso pa Aamori, amene msinkhu wao unanga msinkhu wa mikungudza, nakhala nayo mphamvu ngati thundu; koma ndinaononga zipatso zao m’mwamba, ndi mizu yao pansi.

10 Ndipo ndinakukwezani kuchokera m’dziko la Ejipito, ndi kukutsogolerani zaka makumi anai m’chipululu, kuti mulandire dziko la Aamori likhale cholowa chanu.

11 Ndipo ndinaukitsa mwa ana anu aneneri, ndi mwa anyamata anu Anaziri. Si momwemo, inu ana a Israele, ati Yehova?

12 Koma munamwetsa Anaziri vinyo, ndi kulamulira aneneri ndi kuti, Musamanenera.

13 Taonani, ndidzakupsinjani m’malo mwanu, monga lipsinja galeta lodzala ndi mitolo fwaa.

14 Ndipo populumukirapo padzasowera waliwiro, ndi wamphamvu; sadzalimbikitsa mphamvu yake, ndi ngwazi siidzapulumutsa moyo wake;

15 ndi wokoka uta sadzalimbika, ndi waliwiro sadzadzipulumutsa; ngakhale woyenda pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake;

16 ndi wolimba mtima mwa ngwazi adzathawa wamaliseche tsiku lomwelo, ati Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/2-e43a2d5ebcca96c698a20579f20721a7.mp3?version_id=1068—

Categories
AMOSI

AMOSI 3

Zoipa za Israele; aneneratu kuti adzalangidwa

1 Tamverani mau awa akunenerani Yehova motsutsa, inu ana a Israele, kulinenera banja lonse ndinalikweza kulitulutsa m’dziko la Ejipito, ndi kuti,

2 Inu nokha ndinakudziwani mwa mabanja onse a padziko lapansi, m’mwemo ndidzakulangani chifukwa cha mphulupulu zanu zonse.

3 Kodi awiri adzayenda pamodzi asanapanganiranetu?

4 Kodi mkango udzabangula m’nkhalango wosakhala nayo nyama? Kodi msona wa mkango udzalira m’ngaka mwake usanagwire kanthu?

5 Kodi mbalame idzakodwa mumsampha pansi popanda msampha woitchera? Kodi msampha ufwamphuka pansi wosakola kanthu?

6 Kodi adzaomba lipenga m’mzinda osanjenjemera anthu? Kodi choipa chidzagwera mzinda osachichita Yehova?

7 Pakuti Ambuye Yehova sadzachita kanthu osawulula chinsinsi chake kwa atumiki ake aneneri.

8 Mkango ukabangula, ndani amene saopa? Ambuye Yehova wanena, ndani amene sanenera?

9 Bukitsani kunyumba zachifumu za Asidodi, ndi kunyumba zachifumu za m’dziko la Ejipito, nimuziti, Sonkhanani pa mapiri a Samariya, ndipo penyani masokosero aakulu m’menemo, ndi ozunzika m’kati mwake.

10 Pakuti sadziwa kuchita zolungama, amene akundika zachiwawa ndi umbala m’nyumba zao zachifumu, ati Yehova.

11 Chifukwa chake, atero Ambuye Yehova, Padzakhala mdani pozungulira pake padziko, nadzatsitsa kukuchotsera mphamvu yako; ndi za m’nyumba zako zachifumu adzazifunkha.

12 Atero Yehova, Monga mbusa alanditsa m’kamwa mwa mkango miyendo iwiri, kapena kansonga ka khutu, momwemo adzalanditsidwa ana a Israele okhala pansi mu Samariya, m’ngodya ya guwa logonapo, ndi pa mitsamiro ya kama.

13 Tamverani inu, muchitire umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo, ati Ambuye Yehova Mulungu wa makamu.

14 Pakuti tsiku lakumlanga Israele chifukwa cha zolakwa zake, ndidzalanganso maguwa a nsembe a ku Betele; ndi nyanga za guwa la nsembe zidzadulidwa, ndipo zidzagwa pansi.

15 Ndipo ndidzakantha nyumba ya nyengo yachisanu, pamodzi ndi nyumba ya nyengo yadzuwa; ndi nyumba zaminyanga zidzaonongeka; ndi nyumba zazikuluzo zidzatha, ati Yehova.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/3-413f92e003fc0cd874071cedc4b4a46a.mp3?version_id=1068—

Categories
AMOSI

AMOSI 4

Aisraele adzadulidwa chifukwa cha zoipa ndi kuuma mtima kwao

1 Tamverani mau awa, inu ng’ombe zazikazi za ku Basani, zokhala m’phiri la Samariya, zosautsa aumphawi, zopsinja osowa, zonena kwa ambuyao, Bwerani nacho, timwe.

2 Ambuye Yehova walumbira pali chiyero chake, kuti taonani, adzakugwerani masiku akuti adzakuchotsani ndi zokowera, ndi otsala anu ndi mbedza.

3 Ndipo mudzatulukira popasuka linga, yense m’tsogolo mwake, ndi kutayika ku Harimoni, ati Yehova.

4 Idzani ku Betele, mudzalakwe ku Giligala, nimuchulukitse zolakwa, nimubwere nazo nsembe zanu zophera m’mawa ndi m’mawa, magawo anu akhumi atapita masiku atatuatatu;

5 nimutenthe nsembe zolemekeza zachotupitsa, nimulalikire nsembe zaufulu, ndi kuzimveketsa; pakuti ichi muchikonda, inu ana a Israele, ati Ambuye Yehova.

6 Ndipo Ine ndakupatsaninso mano oyera m’mizinda yanu yonse, ndi kusowa mkate m’malo mwanu monse; koma simunabwerere kudza kwa Ine, ati Yehova.

7 Ndipo Ine ndakumanani mvula, itatsala miyezi itatu isanafika nyengo yakukolola; ndipo ndinavumbitsira mzinda umodzi mvula, osavumbitsira mzinda wina; munda wina unavumbidwa mvula, ndi m’munda mosavumbidwa mvula munafota.

8 M’mwemo mizinda iwiri kapena itatu inayenda peyupeyu kumzinda umodzi kukamwa madzi, koma sanakhute; koma simunabwerere kudza kwa Ine, ati Yehova.

9 Ndinakukanthani ndi chinsikwi ndi chinoni; minda yanu yochuluka yamipesa, ndi yamikuyu, ndi yaazitona, yaonongeka ndi dzombe; koma simunabwerere kudza kwa Ine, ati Yehova.

10 Ndinatumiza mliri pakati panu monga mu Ejipito; anyamata anu ndawapha ndi lupanga, ndi kutenga akavalo anu; ndipo ndinakweretsa kununkha kwa chigono chanu kufikitsa kumphuno kwanu; koma simunabwerere kudza kwa Ine, ati Yehova.

11 Ndinagubuduza ena mwa inu, monga umo Mulungu anagubuduzira Sodomu ndi Gomora; ndipo inu munali ngati muuni wofumulidwa kumoto; koma simunabwerere kudza kwa Ine, ati Yehova.

12 Chifukwa chake ndidzatero nawe, Israele; popeza ndidzakuchitira ichi, dzikonzeretu kukomana ndi Mulungu wako, Israele.

13 Pakuti taona, Iye amene aumba mapiri, nalenga mphepo, nafotokozera munthu maganizo ake, nasanduliza m’mawa ukhale mdima, naponda pa misanje ya dziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova Mulungu wa makamu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/4-c5207feb45d7b96320d57bf4c91c32fd.mp3?version_id=1068—

Categories
AMOSI

AMOSI 5

Nyimbo ya maliro yakunena za kuthyola kwa Israele

1 Tamverani mau awa ndinenawa, akhalire inu nyimbo ya maliro, nyumba ya Israele inu.

2 Namwali wa Israele wagwa, sadzaukanso; wagwetsedwa pa nthaka yake, palibe womuutsa.

3 Pakuti atero Ambuye Yehova, M’nyumba ya Israele, mzinda wotulukamo chikwi chimodzi adzautsalira zana limodzi, ndi uwu wotulukamo zana limodzi adzautsalira khumi.

4 Pakuti atero Yehova kwa nyumba ya Israele, Mundifunefune Ine, ndipo mudzakhala ndi moyo;

5 koma musamafuna Betele, kapena kumalowa mu Giligala; musamapita ku Beereseba; pakuti Giligala adzalowadi m’ndende, ndi Betele adzasanduka chabe.

6 Funani Yehova, ndipo mudzakhala ndi moyo; angabuke ngati moto m’nyumba ya Yosefe, ndipo unganyeke wopanda wakuzima mu Betele;

7 inu osintha chiweruzo chikhale chivumulo, nimugwetsa pansi chilungamo.

8 Iye wakulenga Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, nasanduliza mdima wandiweyani ukhale m’mawa, nasanduliza usana ude ngati usiku, wakuitana madzi a m’nyanja, nawatsanulira padziko lapansi, dzina lake ndiye Yehova;

9 wakufikitsa chionongeko pa wamphamvu modzidzimuka, kuti chionongekocho chigwere linga.

10 Iwo adana naye wodzudzula kuchipata, nanyansidwa naye wolunjikitsa mau.

11 Popeza tsono mupondereza aumphawi, ndi kumsonkhetsa tirigu; mwamanga nyumba za miyala yosema, koma simudzakhala m’mwemo; mwaoka minda ya mipesa yokonda, koma simudzamwa vinyo wake.

12 Pakuti ndidziwa kuti zolakwa zanu nzochuluka, ndi machimo anu ndi olimba, inu akusautsa olungama, akulandira chokometsera mlandu, akukankha osowa kuchipata.

13 Chifukwa chake wochenjerayo akhala chete nthawi yomweyo; pakuti ndiyo nthawi yoipa.

14 Funani chokoma, si choipa ai; kuti mukhale ndi moyo; motero Yehova Mulungu wa makamu adzakhala ndi inu, monga munena.

15 Danani nacho choipa, nimukonde chokoma; nimukhazikitse chiweruzo kuchipata; kapena Yehova Mulungu wa makamu adzachitira chifundo otsala a Yosefe.

16 Chifukwa chake atero Yehova, Mulungu wa makamu, Ambuye, M’makwalala onse mudzakhala kulira, ndi m’miseu yonse adzati, Kalanga ine! Kalanga ine! Nadzaitana wakumunda adze kumaliro, ndi odziwa maliridwe a nthetemya alire.

17 Ndi m’minda yonse yamipesa mudzakhala kulira, pakuti ndipita pakati pako, ati Yehova.

18 Tsoka inu akufuna tsiku la Yehova? Mudzapindulanji nalo tsiku la Yehova? Ndilo mdima, si kuunika ai.

19 Kudzakhala monga munthu akathawa mkango, ndi chimbalangondo chikomana naye; kapena akalowa m’nyumba, natsamira kukhoma ndi dzanja lake, nimluma njoka.

20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala la mdima, si la kuunika ai? Lakuda bii, lopanda kuwala m’menemo?

21 Ndidana nao, ndinyoza zikondwerero zanu, sindidzakondwera nayo misonkhano yanu yoletsa.

22 Inde, mungakhale mupereka kwa Ine nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zaufa, sindidzazilandira Ine; ndi nsembe zoyamika za ng’ombe zanu zonenepa, sindidzazisamalira Ine.

23 Mundichotsere phokoso la nyimbo zanu; sindifuna kumva mayimbidwe a zisakasa zanu.

24 Koma chiweruzo chiyende ngati madzi, ndi chilungamo ngati mtsinje wosefuka.

25 Ngati munabwera nazo kwa Ine nsembe zophera ndi zaufa zaka makumi anai m’chipululu, inu nyumba ya Israele?

26 Inde mwasenza hema wa mfumu yanu, ndi tsinde la mafano anu, nyenyezi ya mulungu wanu, amene mudadzipangira.

27 M’mwemo ndidzakutengani kunka nanu kundende kutsogolo kwa Damasiko, ati Yehova, amene dzina lake ndiye Mulungu wa makamu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/5-3f7b752f02711839e9893b47ce6cb756.mp3?version_id=1068—

Categories
AMOSI

AMOSI 6

Aisraele otsata zilakolako zao adzapsinjika ndi mtundu wina wa anthu

1 Tsoka osalabadirawo muZiyoni, ndi iwo okhazikika m’phiri la Samariya, ndiwo anthu omveka a mtundu woposa wa anthu, amene nyumba ya Israele iwafikira!

2 Pitani ku Kaline, nimuone; kuchokera komweko mupite ku Hamati wamkulu mutsikire ku Gati wa Afilisti; kodi awo ndi okoma koposa maufumu ano? Kapena malire ao aposa malire anu?

3 Inu akutalikitsa tsiku loipa, ndi kusendeza pafupi mpando wachiwawa;

4 ogona pamakama aminyanga, nadzithinula pa maguwa ao ogonapo, nadya anaankhosa a kuzoweta, ndi anaang’ombe ochoka pakati pa khola;

5 akungoimba kutsata maliridwe a zeze, nadzilingiririra zoimbira nazo ngati Davide;

6 akumwera vinyo m’zipanda, nadzidzoza ndi mafuta abwino oposa, osagwidwa chisoni ndi kuthyoka kwa Yosefe.

7 Chifukwa chake tsono, adzatengedwa ndende ndi oyamba kutengedwa ndende; ndi phokoso la iwo odzithinula lidzapita.

8 Ambuye Yehova walumbira pali Iye mwini, ati Yehova Mulungu wa makamu, Ndinyansidwa nako kudzikuza kwa Yakobo, ndidana nazo nyumba zake zachifumu; m’mwemo ndidzapereka mzinda, ndi zonse zili m’menemo.

9 Ndipo kudzachitika, mukatsala amuna khumi m’nyumba imodzi, adzafa.

10 Ndipo mbale wake wa munthu akamnyamula, ndiye womtentha, kutulutsa mafupa m’nyumba, nakati kwa iye ali m’kati mwa nyumbamo, Atsala wina nawe kodi? Nakati Iai; pamenepo adzati, Khala chete; pakuti sitingatchule dzina la Yehova.

11 Pakuti taonani, Yehova walamulira, nadzakantha nyumba yaikulu ichite mpata, ndi nyumba yaing’ono ichite mindala.

12 Kodi akavalo adzathamanga pathanthwe? Kodi adzalimako ndi ng’ombe pakuti mwasanduliza chiweruzo chikhale ndulu, ndi chipatso cha chilungamo chikhale chivumulo;

13 inu okondwera nacho chopanda pake, ndi kuti, Kodi sitinadzilimbitse tokha ndi kulanda Karinaimu mwa mphamvu yathuyathu?

14 Pakuti taonani, ndidzakuutsirani mtundu wa anthu, nyumba ya Israele, ati Yehova Mulungu wa makamu; ndipo adzakupsinjani kuyambira polowera ku Hamati kufikira mtsinje wa kuchidikha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/6-6c5f530b18b73ef358a1f1f30e54dbdd.mp3?version_id=1068—

Categories
AMOSI

AMOSI 7

Masomphenya atatu, dzombe, moto wonyambita, ndi chingwe cholungamitsa chilili

1 Ambuye Yehova anandionetsa chotere; ndipo taonani, anaumba dzombe, poyamba kuphuka kwa udzu wa chibwereza; ndipo taonani, ndicho chibwereza atawusengera mfumu.

2 Ndipo kunachitika m’mene lidatha kudya msipu wa dziko, ndinati, Ambuye Yehova, khululukiranitu Yakobo; adzakhala chilili bwanji? Popeza ndiye wamng’ono.

3 Ndipo Yehova anachileka. Sichidzachitika, ati Yehova.

4 Ambuye Yehova anandionetsa chotere; ndipo taonani, Ambuye Yehova anaitana kuti atsutse ndi moto; ndipo unanyambita chakuya chachikulu ukadanyambitanso dziko.

5 Pamenepo ndinati, Ambuye Yehova, lekanitu; Yakobo adzakhala chilili bwanji? Pakuti ali wamng’ono.

6 Ndipo Yehova anachileka. Ichi chomwe sichidzachitika, ati Ambuye Yehova.

7 Anandionetsa chotere; ndipo taonani, Ambuye anaima pa khoma lomangidwa ndi chingwe cholungamitsira chilili; ndi chingwe cholungamitsira chilili m’dzanja lake.

8 Ndipo Yehova anati kwa ine, Amosi, uona chiyani? Ndipo ndinati, Chingwe cholungamitsira chilili. Nati Ambuye, Taona, ndidzaika chingwe cholungamitsira chilili pakati pa anthu anga Israele, sindidzawalekanso:

9 ndi misanje ya Isaki idzakhala bwinja; ndi malo opatulika a Israele adzapasuka; ndipo ndidzaukira nyumba ya Yerobowamu ndi lupanga.

Amosi ndi Amaziya atsutsana ku Betele

10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Betele anatumiza kwa Yerobowamu mfumu ya Israele, ndi kuti, Amosi wapangira inu chiwembu pakati pa nyumba ya Israele; dziko silingathe kulola mau ake onse.

11 Pakuti atero Amosi, Yerobowamu adzafa ndi lupanga, ndi Israele adzatengedwadi ndende, kuchoka m’dziko lake.

12 Amaziya anatinso kwa Amosi, Mlauli iwe, choka, thawira kudziko la Yuda, nudye, nunenere komweko;

13 koma usaneneranso ku Betele; pakuti pamenepo mpamalo opatulika a mfumu, ndiyo nyumba yachifumu.

14 Pamenepo Amosi anayankha, nati kwa Amaziya, Sindinalimneneri, kapena mwana wa mneneri, koma ndinali woweta ng’ombe, ndi wakutchera nkhuyu;

15 ndipo Yehova ananditenga ndilikutsata nkhosa, nati kwa ine Yehova, Muka, nenera kwa anthu anga Israele.

16 Chifukwa chake tsono, tamvera mau a Yehova, Iwe ukuti, Usamanenera chotsutsana ndi Israele, usadonthetsa mau akutsutsana ndi nyumba ya Isaki;

17 chifukwa chake atero Yehova, Mkazi wako adzakhala wadama m’mzinda, ndi ana ako aamuna ndi aakazi adzagwa ndi lupanga, ndi dziko lako lidzagawanidwa ndi kuyesa chingwe, ndi iwe mwini udzafa m’dziko lodetsedwa; ndipo Israele adzatengedwadi ndende kuchoka m’dziko lake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/7-861a86eaeb1f9faf748a3a72b42db9e9.mp3?version_id=1068—

Categories
AMOSI

AMOSI 8

Masomphenya a dengu la zipatso. Zoopsa za pa Israele

1 Ambuye Yehova anandionetsa chotere; ndipo taonani, dengu la zipatso zamalimwe.

2 Ndipo anati, Amosi uona chiyani? Ndipo ndinati, Dengu la zipatso zamalimwe. Nati Yehova kwa ine, Chitsiriziro chafikira anthu anga Israele, sindidzawalekanso.

3 Koma nyimbo za ku Kachisi zidzasanduka kubuma tsiku ilo, ati Ambuye Yehova; mitembo idzachuluka; adzaitaya paliponse padzakhala zii.

4 Tamverani ichi, inu akumeza aumphawi, ndi kuwatha ofatsa m’dziko, ndi kuti,

5 Mwezi wokhala upita liti, kuti tigulitse dzinthu? NdiSabata, kuti titsegulire tirigu? Ndi kuchepsa efa, ndi kukulitsa sekeli, ndi kuchenjerera nayo miyeso yonyenga;

6 kuti tigule osauka ndi ndalama, ndi aumphawi ndi nsapato, ndi kugulitsa nsadwa za tirigu.

7 Yehova walumbira pali kudzikuza kwa Yakobo, Ngati ndidzaiwala konse ntchito zao zilizonse?

8 Kodi dziko silidzanjenjemera chifukwa cha ichi, ndi kulira aliyense wokhalamo? Inde lidzakwera lonseli ngati madzi a m’mtsinje; lidzagwezeka, ndi kutsikanso ngati mtsinje wa Ejipito.

9 Ndipo kudzachitika tsiku lomwelo, ati Ambuye Yehova, ndidzalowetsa dzuwa usana, ndi kudetsa dziko pausana poyera.

10 Ndipo ndidzasanduliza zikondwerero zanu zikhale maliro, ndi nyimbo zanu zikhale za maliro, ndi kufikitsa ziguduli m’chuuno monse, ndi mpala pamutu uliwonse; nadzakhala ngati maliro a mwana mmodzi yekha, ndi chitsiriziro chake ngati tsiku lowawa.

11 Taonani, akudza masiku, ati Ambuye Yehova, akuti ndidzatumiza njala m’dzikomo, si njala ya mkate kapena ludzu la madzi, koma njala ya kumva mau a Yehova.

12 Ndipo adzayendayenda peyupeyu kuyambira kunyanja kufikira kunyanja ndi kuyambira kumpoto kufikira kum’mawa; adzathamangathamanga kufunafuna mau a Yehova, koma osawapeza.

13 Tsiku lomwelo anamwali okongola ndi anyamata adzakomoka nalo ludzu.

14 Iwo akulumbira ndi kutchula tchimo la Samariya, ndi kuti, Pali Mulungu wako, Dani; ndipo, Pali moyo wa njira ya ku Beereseba, iwowa adzagwa, osaukanso konse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/8-10304912781a25be78b9a4012bc934ac.mp3?version_id=1068—

Categories
AMOSI

AMOSI 9

Masomphenya a kulangidwa koopsa

1 Ndinaona Ambuye alikuima paguwa la nsembe, nati Iye, Kantha mitu ya nsanamira, kuti ziundo zigwedezeke; nuphwanye mitu yao yonse; ndipo ndidzapha otsiriza ao ndi lupanga; wothawayo mwa iwo sadzathawadi, ndi wopulumukayo mwa iwo sadzapulumukadi.

2 Angakhale akumba mpaka kunsi kwa manda, dzanja langa lidzawatenga kumeneko; angakhale akwera kumwamba, ndidzawatsitsa komweko.

3 Angakhale abisala pamwamba pa Karimele, ndidzawapwaira ndi kuwatenga komweko; angakhale abisala pamaso panga pansi pa nyanja, kumeneko ndidzalamulira njoka, ndipo idzawaluma.

4 Angakhale alowa ndende pamaso pa adani ao, kumeneko ndidzalamulira lupanga, ndipo lidzawapha; ndipo ndidzayang’anitsa maso anga kwa iwowa, kuwachitira choipa, si chokoma ai.

5 Pakuti Ambuye Yehova wa makamu ndiye amene akhudza dziko, nilisungunuka; ndi onse okhalamo adzachita maliro; ndipo lidzakwera lonseli ngati madzi a m’mtsinje; nilidzatsikanso ngati mtsinje wa mu Ejipito;

6 ndiye amene amanga zipinda zake zosanja m’mwamba, nakhazika tsindwi lake padziko lapansi; Iye amene aitana madzi a m’nyanja, nawatsanulira padziko; dzina lake ndiye Yehova.

7 Kodi simukhala kwa Ine ngati ana a Kusi, inu ana a Israele? Ati Yehova. Sindinakweza Israele ndine, kumtulutsa m’dziko la Ejipito, ndi Afilisti ku Kafitori, ndi Aaramu ku Kiri?

8 Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wochimwawo, ndipo ndidzauononga kuuchotsa padziko lapansi; pokhapo sindidzaononga nyumba ya Yakobo kuitha konse, ati Yehova.

9 Pakuti taonani, ndidzalamulira, ndipo ndidzapeta nyumba ya Israele mwaamitunduonse, monga apeta tirigu m’lichero; koma silidzagwa pansi diso, ndi limodzi lonse.

10 Ochimwa onse a anthu anga adzafa ndi lupanga, ndiwo amene akuti, Choipa sichidzatipeza, kapena kutidulira.

Lonjezo kuti madalitso adzabwera

11 Tsiku lomwelo ndidzautsa msasa wa Davide udagwawo, ndi kukonzanso zopasuka zake; ndipo ndidzautsa zogumuka zake, ndi kuumanga monga masiku a kalelo;

12 kuti alandire otsala a Edomu akhale cholowa chao, ndi amitundu onse a kutchedwa dzina langa, ati Yehova wakuchita izi.

13 Taonani, akudza masiku, ati Yehova, akuti wolima adzapezana ndi wodula, ndi woponda mphesa adzapezana ndi wofetsa, ndi mapiri adzakhetsa vinyo watsopano, ndi zitunda zonse zidzasungunuka.

14 Ndipo ndidzabwezanso undende wa anthu anga Israele, ndipo adzamanganso mizinda ya mabwinja, ndi kukhala m’menemo; nadzaoka minda ya mipesa nadzamwa vinyo wake, nadzalima minda ndi kudya zipatso zake.

15 Ndipo ndidzawaoka m’dziko mwao ndipo sadzazulidwanso m’dziko lao limene ndawapatsa, ati Yehova Mulungu wako.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/AMO/9-b2d22ee4e200fea8de37ea6469b1aa25.mp3?version_id=1068—