Categories
AKOLOSE

AKOLOSE Mau Oyamba

Mau Oyamba

Kolose unali mzinda wina wa ku Asiya, kuvuma kwa Efeso. Paulo si amene adayambitsa mpingo kumeneko, komabe amausamala, poti adatuma anthu ake ku Koloseko kuchokera ku Efeso. Paulo anamva kuti aphunzitsi ena onyenga akusokoneza mpingo umenewo; iwo akuti ofuna kumdziwa Mulungu ndi kupulumuka ayenera kupembedza mafumu ndi akuluakulu akumwamba, ayeneranso kuumbalidwa ndi kutsata miyambo ndi malamulo ena okhudza zakudya ndi zina zotere.

Tsono Paulo awalembera kalatayi kuti atsutse zabodzazi pofotokoza uthenga weniweni wa Chikhristu, makamaka izi zakuti Yesu Khristu yekha ali ndi mphamvu zopulumutsira anthu, koma zimene amalalika aphunzitsi aja zimangosokoneza anthu ndi kuwalekanitsa ndi Khristu. Mulungutu adalenga zinthu zonse kudzera mwa Khristu ndipo amabwezera zonsezo kwa Iye mwini wake kudzera mwa Khristu yemweyo. Anthu a padziko lonse lapansi angayembekeze kupulumuka pokhapo atakhala mwa Khristu ndi kumaphatikana naye. Zotsatira zake nzakuti iwowo aongolere moyo wao potsata zomwe iye Paulo akuwaphunzitsazi.

Potuma Titiko ku Filipi kuti akapereke kalatayi, Paulo atumanso mnyamata wina womperekeza, dzina lake Onesimo; ameneyu ndiye kapolo uja amene nkhani yake ipezeka m’kalata yomwe Paulo adalembera Filemoni.

Za mkatimu

Mau oyamba 1.1-8

Za makhalidwe ndi ntchito za Khristu 1.9—2.19

Za moyo watsopano wokhala mwa Khristu 2.20—4.6

Mau otsiriza 4.7-18

Categories
AKOLOSE

AKOLOSE 1

1 Paulo,mtumwiwaKhristuYesu mwa chifuniro cha Mulungu, ndi Timoteo mbaleyo,

2 kwa oyera mtima ndi abale okhulupirika mwa Khristu a mu Kolose: Chisomo kwa inu ndi mtendere wochokera kwa Mulungu Atate wathu.

Za chikhulupiriro ndi chikondano cha a ku Kolose. Paulo awapempherera. Yesu Khristu ali maonekedwe a Mulungu wolenga zonse, mutu wa Mpingo

3 Tiyamika Mulungu Atate wa Ambuye wathu YesuKhristundi kupempherera inu nthawi zonse,

4 popeza tidamva za chikhulupiriro chanu cha mwa Khristu Yesu, ndi chikondi muli nacho kwa oyera mtima onse;

5 chifukwa cha chiyembekezo chosungikira kwa inu mu Mwamba, chimene mudachimva kale m’mau a choonadi cha Uthenga Wabwino,

6 umene udafikira kwa inu; monganso m’dziko lonse lapansi umabala zipatso, numakula, monganso mwa inu, kuyambira tsikulo mudamva nimunazindikira chisomo cha Mulungu m’choonadi;

7 monga momwe munaphunzira kwa Epafra kapolo mnzathu wokondedwa, ndiye mtumiki wokhulupirika wa Khristu chifukwa cha ife;

8 amenenso anatifotokozera chikondi chanu mwa Mzimu.

9 Mwa ichi ifenso, kuyambira tsiku limene tidamva, sitileka kupembedzera ndi kupempherera inu, kuti mukadzazidwe ndi chizindikiritso cha chifuniro chake mu nzeru zonse ndi chidziwitso cha mzimu,

10 kuti mukayenda koyenera Ambuye kukamkondweretsa monsemo, ndi kubala zipatso mu ntchito yonse yabwino, ndi kukula m’chizindikiritso cha Mulungu;

11 olimbikitsidwa m’chilimbiko chonse, monga mwa mphamvu ya ulemerero wake, kuchitira chipiriro chonse ndi kuleza mtima konse pamodzi ndi chimwemwe,

12 ndi kuyamika Atate, amene anatiyeneretsa ife kulandirana nao cholowa cha oyera mtima m’kuunika;

13 amene anatilanditsa ife kuulamuliro wa mdima, natisunthitsa kutilowetsa mu ufumu wa Mwana wa chikondi chake;

14 amene tili nao maomboledwe mwa Iye, m’kukhululukidwa kwa zochimwa zathu;

15 amene ali fanizo la Mulungu wosaonekayo, wobadwa woyamba wa chilengedwe chonse;

16 pakuti mwa Iye, zinalengedwa zonse za m’mwamba, ndi za padziko, zooneka ndi zosaonekazo, kapena mipando yachifumu, kapena maufumu, kapena maukulu, kapena maulamuliro; zinthu zonse zinalengedwa mwa Iye ndi kwa Iye.

17 Ndipo Iye ali woyamba wa zonse, ndipo zonse zigwirizana pamodzi mwa Iye.

18 Ndipo Iye ali mutu wa thupi, Mpingowo; ndiye chiyambi, wobadwa woyamba wotuluka mwa akufa; kuti akakhale Iye mwa zonse woyambayamba.

19 Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa Iye chidzalo chonse chikhalire,

20 mwa Iyenso kuyanjanitsa zinthu zonse kwa Iye mwini, atachita mtendere mwa mwazi wa mtanda wake; mwa Iyetu, kapena za padziko, kapena za mu Mwamba.

21 Ndipo inu, okhala alendo kale ndi adani m’chifuwa chanu m’ntchito zoipazo,

22 koma tsopano anakuyanjanitsani m’thupi lake mwa imfayo, kukaimika inu oyera, ndi opanda chilema ndi osatsutsika pamaso pake;

23 ngatitu, mukhalabe m’chikhulupiriro, ochilimika ndi okhazikika ndi osasunthika kulekana nacho chiyembekezo cha Uthenga Wabwino umene mudaumva, wolalikidwa cholengedwa chonse cha pansi pa thambo; umene ine Paulo ndakhala mtumiki wake.

Machitachita a Paulo mu utumiki wake

24 Tsopano ndikondwera nazo zowawazo chifukwa cha inu, ndipo ndikwaniritsa zoperewera za chisautso cha Khristu m’thupi langa chifukwa cha thupi lake, ndilo Mpingowo;

25 amene ndinakhala mtumiki wake, monga mwa udindo wa Mulungu umene anandipatsa ine wakuchitira inu, wakukwaniritsa mau a Mulungu,

26 ndiwo chinsinsicho chinabisika kuyambira pa nthawizo, ndi kuyambira pa mibadwoyo; koma anachionetsa tsopano kwa oyera mtima ake,

27 kwa iwo amene Mulungu anafuna kuwazindikiritsa ichi chimene chili chuma cha ulemerero wa chinsinsi pakati paamitundu, ndiye Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero;

28 amene timlalikira ife, ndi kuchenjeza munthu aliyense ndi kuphunzitsa munthu aliyense mu nzeru zonse, kuti tionetsere munthu aliyense wamphumphu mwa Khristu;

29 kuchita ichi ndidzivutitsa ndi kuyesetsa monga mwa machitidwe ake akuchita mwa ine ndi mphamvu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/COL/1-af9ee1f2352534de984b6d2c0c2545e8.mp3?version_id=1068—

Categories
AKOLOSE

AKOLOSE 2

1 Pakuti ndifuna kuti inu mudziwe nkhawa imene ndili nayo chifukwa cha inu, ndi iwowa a mu Laodikea, ndi onse amene sanaone nkhope yanga m’thupi;

2 kuti itonthozeke mitima yao, nalumikizike pamodzi iwo m’chikondi, kufikira chuma chonse cha chidzalo cha chidziwitso, kuti akazindikire iwo chinsinsi cha Mulungu, ndiyeKhristu,

3 amene zolemera zonse za nzeru ndi chidziwitso zibisika mwa Iye.

Asatsate ziphunzitso zonyenga

4 Ichi ndinena, kuti munthu asakusokeretseni inu ndi mau okopakopa.

5 Pakuti ndingakhale ndili kwina m’thupi, komatu mumzimu ndili pamodzi ndi inu, wokondwera pakupenya makonzedwe anu, ndi chilimbiko cha chikhulupiriro chanu cha kwa Khristu.

6 Chifukwa chake monga momwe munalandira Khristu Yesu Ambuye, muyende mwa Iye,

7 ozika mizu ndi omangiririka mwa Iye, ndi okhazikika m’chikhulupiriro, monga munaphunzitsidwa, ndi kuchulukitsa chiyamiko.

8 Penyani kuti pasakhale wina wakulanda inu ngati chuma, mwa kukonda nzeru kwake, ndi chinyengo chopanda pake, potsata mwambo wa anthu, potsata zoyamba za dziko lapansi, osati potsata Khristu;

9 pakuti mwa Iye chikhalira chidzalo cha Umulungu m’thupi,

10 ndipo muli odzazidwa mwa Iye, ndiye mutu wa ukulu wonse ndi ulamuliro;

11 amenenso munadulidwa mwa Iye ndi mdulidwe wosachitika ndi manja, m’mavulidwe a thupi, mumdulidwewa Khristu;

12 popeza munaikidwa m’manda pamodzi ndi Iye muubatizo, momwemonso munaukitsidwa pamodzi ndi Iye m’chikhulupiriro cha machitidwe a Mulungu, amene anamuukitsa Iye kwa akufa.

13 Ndipo inu, pokhala akufa m’zolakwa ndi kusadulidwa kwa thupi lanu, anakupatsani moyo pamodzi ndi Iye, m’mene adatikhululukira ife zolakwa zonse;

14 adatha kutifafanizira cha pa ifecho cholembedwa m’zoikikazo, chimene chinali chotsutsana nafe: ndipo anachichotsera pakatipo, ndi kuchikhomera ichi pamtanda;

15 atavula maukulu ndi maulamuliro, anawaonetsera poyera, nawagonjetsera nako.

16 Chifukwa chake munthu aliyense asakuweruzeni inu m’chakudya, kapena chakumwa, kapena m’kunena tsiku la chikondwerero, kapena tsiku lokhala mwezi, kapena laSabata;

17 ndizo mthunzi wa zilinkudzazo; koma thupi ndi la Khristu.

18 Munthu aliyense asakunyengeni ndi kulanda mphotho yanu ndi kudzichepetsa mwini wake, ndi kugwadira kwaangelo, ndi kukhalira mu izi adaziona, wodzitukumula chabe ndi zolingalira za thupi lake, wosagwiritsa mutuwo,

19 kuchokera kwa Iye amene thupi lonse, lothandizidwa ndi kulumikizidwa pamodzi mwa mfundo ndi mitsempha, likula ndi makulidwe a Mulungu.

20 Ngati munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nazo zoyamba za dziko lapansi, mugonjeranji kuzoikikazo, monga ngati moyo wanu mukhala nao m’dziko lapansi,

21 usaikapo dzanja, usalawa, usakhudza,

22 (ndizo zonse zakuonongedwa pochita nazo), monga mwa malangizo ndi maphunziro a anthu?

23 Zimene zili naotu manenedwe a nzeru m’kutumikira kwa chifuniro cha mwini wake, ndi kudzichepetsa, ndi kusalabadira thupi; koma zilibe mphamvu konse yakuletsa chikhutitso cha thupi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/COL/2-200496f5d3547476493b061eaa284529.mp3?version_id=1068—

Categories
AKOLOSE

AKOLOSE 3

Atsate kuyeramtima, ndi chikondano cha pa abale

1 Chifukwa chake ngati munaukitsidwa pamodzi ndiKhristu, funani zakumwamba, kumene kuli Khristu wokhala padzanja lamanja la Mulungu.

2 Lingalirani zakumwamba osati za padziko ai.

3 Pakuti munafa, ndipo moyo wanu wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu.

4 Pamene Khristu adzaoneka, ndiye moyo wathu, pamenepo inunso mudzaonekera pamodzi ndi Iye mu ulemerero.

5 Chifukwa chake fetsani ziwalozo zili padziko; dama, chidetso, chifunitso chamanyazi, chilakolako choipa, ndi chisiriro, chimene chili kupembedza mafano;

6 chifukwa cha izi zomwe ukudza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera;

7 zimene munayendamo inunso kale, pamene munakhala ndi moyo wanu m’menemo.

8 Koma tsopano tayani inunso zonsezi: mkwiyo, kupsa mtima, dumbo, mwano, zonyansa zotuluka m’kamwa mwanu:

9 musamanamizana wina ndi mnzake; popeza mudavula munthu wakale pamodzi ndi ntchito zake,

10 ndipo munavala watsopano, amene alikukonzeka watsopano, kuti akhale nacho chizindikiritso, monga mwa chifaniziro cha Iye amene anamlenga iye;

11 pamene palibe Mgriki ndi Ayuda,mdulidwendi kusadulidwa, watchedwa wakunja, Msukuti, kapolo, mfulu, komatu Khristu ndiye zonse, ndi m’zonse.

12 Chifukwa chake valani, monga osankhika a Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa, mtima wachifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, chifatso, kuleza mtima;

13 kulolerana wina ndi mnzake, ndi kukhululukirana eni okha, ngati wina ali nacho chifukwa pa mnzake; monganso Ambuye anakhululukira inu, teroni inunso;

14 koma koposa izi zonse khalani nacho chikondano, ndicho chomangira cha mtima wamphumphu.

15 Ndipo mtendere wa Khristu uchite ufumu m’mitima yanu, kulingakonso munaitanidwa m’thupi limodzi; ndipo khalani akuyamika.

16 Mau a Khristu akhalitse mwa inu chichulukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalimo, ndi mayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuimbira Mulungu ndi chisomo mumtima mwanu.

17 Ndipo chilichonse mukachichita m’mau kapena muntchito, chitani zonse m’dzina la Ambuye Yesu, ndi kuyamika Mulungu Atate mwa Iye.

Za banja la munthu

18 Akazi inu, muzimvera amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.

19 Amuna inu, kondani akazi anu, ndipo musawawire mtima iwo.

20 Ana inu, mverani akubala inu m’zonse, pakuti ichi Ambuye akondwera nacho.

21 Atate inu, musaputa ana anu, kuti angataye mtima.

22 Akapolo inu, mverani m’zonse iwo amene ali ambuye monga mwa thupi, wosati ukapolo wa pamaso, monga okondweretsa anthu, komatu ndi mtima wakulinga kumodzi, akuopa Ambuye;

23 chilichonse mukachichita, gwirani ntchito mochokera mumtima, monga kwa Ambuye, osati kwa anthu ai;

24 podziwa kuti mudzalandira kwa Ambuye mphotho ya cholowa; mutumikira Ambuye Khristu mwaukapolo.

25 Pakuti iye wakuchita chosalungama adzalandiranso chosalungama anachitacho; ndipo palibe tsankho.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/COL/3-30da9d2e9a6fcfff941d7b5f91ccc5c6.mp3?version_id=1068—

Categories
AKOLOSE

AKOLOSE 4

1 Ambuye inu, chitirani akapolo anu cholungama ndi cholingana; podziwa kuti inunso muli naye Mbuye mu Mwamba.

Awachenjeza za kupemphera ndi za kukhala nayo nzeru

2 Chitani khama m’kupemphera, nimudikire momwemo ndi chiyamiko;

3 ndi kutipempherera ifenso pomwepo, kuti Mulungu atitsegulire ife pakhomo pa mau, kuti tilankhule chinsinsi chaKhristu; chimenenso ndikhalira m’ndende,

4 kuti ndichionetse ichi monga ndiyenera kulankhula.

5 Muyendere munzeru ndi iwo akunja, kuchita machawi nthawi ingatayike.

6 Mau anu akhale m’chisomo, okoleretsa, kuti mukadziwe inu mayankhidwe anu a kwa yense akatani.

Atumidwa Tikiko ndi Onesimo

7 Zonse za kwa ine adzakuzindikiritsani Tikiko, mbale wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika ndi kapolo mnzanga mwa Ambuye:

8 amene ndamtuma kwa inu chifukwa cha ichi chomwe, kuti mukazindikire za kwa ife, ndi kuti atonthoze mitima yanu;

9 pamodzi ndi Onesimo, mbale wokhulupirika ndi wokondedwa, amene ali wa kwa inu. Zonse za kuno adzakuzindikiritsani inu.

Malonje

10 Aristariko wam’ndende mnzanga akupatsani moni, ndi Marko, msuweni wa Barnabasi (amene munalandira zolamulira za kwa iye; akafika kwanu, mumlandire iye),

11 ndi Yesu, wotchedwa Yusto, ndiwo amdulidwe; iwo okha ndiwo antchito anzanga a mu Ufumu wa Mulungu, ndiwo akundikhalira ine chonditonthoza mtima.

12 Akupatsani moni Epafra ndiye wa kwa inu, ndiye kapolo wa Khristu Yesu, wakulimbika m’mapemphero ake masiku onse chifukwa cha inu, kuti mukaime amphumphu ndi odzazidwa m’chifuniro chonse cha Mulungu.

13 Pakuti ndimchitira iye umboni kuti adziwawitsa nayo ntchito chifukwa cha inu, ndi iwo a mu Laodikea, ndi iwo a mu Hierapoli.

14 Akupatsani moni Luka sing’anga wokondedwa, ndi Dema.

15 Perekani moni kwa abalewo a mu Laodikea, ndi Nimfa, ndiMpingowo wa m’nyumba yao.

16 Ndipo pamene mudamwerenga kalata iyi, amwerengenso mu Mpingo wa ku Laodikea, ndi inunso muwerenge wa ku Laodikea.

17 Ndipo nenani kwa Arkipo, Samaliratu utumiki umene udaulandira mwa Ambuye, kuti uukwanitse.

18 Ndipereka moni ndi dzanja langa, kwa ine Paulo. Kumbukirani zomangira zanga. Chisomo chikhale nanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/COL/4-33250c00bc42ae07f64c5c3c2aefad5d.mp3?version_id=1068—