1 Paulo,mtumwiwaKhristuYesu mwa chifuniro cha Mulungu, ndi Timoteo mbaleyo,
2 kwa oyera mtima ndi abale okhulupirika mwa Khristu a mu Kolose: Chisomo kwa inu ndi mtendere wochokera kwa Mulungu Atate wathu.
Za chikhulupiriro ndi chikondano cha a ku Kolose. Paulo awapempherera. Yesu Khristu ali maonekedwe a Mulungu wolenga zonse, mutu wa Mpingo
3 Tiyamika Mulungu Atate wa Ambuye wathu YesuKhristundi kupempherera inu nthawi zonse,
4 popeza tidamva za chikhulupiriro chanu cha mwa Khristu Yesu, ndi chikondi muli nacho kwa oyera mtima onse;
5 chifukwa cha chiyembekezo chosungikira kwa inu mu Mwamba, chimene mudachimva kale m’mau a choonadi cha Uthenga Wabwino,
6 umene udafikira kwa inu; monganso m’dziko lonse lapansi umabala zipatso, numakula, monganso mwa inu, kuyambira tsikulo mudamva nimunazindikira chisomo cha Mulungu m’choonadi;
7 monga momwe munaphunzira kwa Epafra kapolo mnzathu wokondedwa, ndiye mtumiki wokhulupirika wa Khristu chifukwa cha ife;
8 amenenso anatifotokozera chikondi chanu mwa Mzimu.
9 Mwa ichi ifenso, kuyambira tsiku limene tidamva, sitileka kupembedzera ndi kupempherera inu, kuti mukadzazidwe ndi chizindikiritso cha chifuniro chake mu nzeru zonse ndi chidziwitso cha mzimu,
10 kuti mukayenda koyenera Ambuye kukamkondweretsa monsemo, ndi kubala zipatso mu ntchito yonse yabwino, ndi kukula m’chizindikiritso cha Mulungu;
11 olimbikitsidwa m’chilimbiko chonse, monga mwa mphamvu ya ulemerero wake, kuchitira chipiriro chonse ndi kuleza mtima konse pamodzi ndi chimwemwe,
12 ndi kuyamika Atate, amene anatiyeneretsa ife kulandirana nao cholowa cha oyera mtima m’kuunika;
13 amene anatilanditsa ife kuulamuliro wa mdima, natisunthitsa kutilowetsa mu ufumu wa Mwana wa chikondi chake;
14 amene tili nao maomboledwe mwa Iye, m’kukhululukidwa kwa zochimwa zathu;
15 amene ali fanizo la Mulungu wosaonekayo, wobadwa woyamba wa chilengedwe chonse;
16 pakuti mwa Iye, zinalengedwa zonse za m’mwamba, ndi za padziko, zooneka ndi zosaonekazo, kapena mipando yachifumu, kapena maufumu, kapena maukulu, kapena maulamuliro; zinthu zonse zinalengedwa mwa Iye ndi kwa Iye.
17 Ndipo Iye ali woyamba wa zonse, ndipo zonse zigwirizana pamodzi mwa Iye.
18 Ndipo Iye ali mutu wa thupi, Mpingowo; ndiye chiyambi, wobadwa woyamba wotuluka mwa akufa; kuti akakhale Iye mwa zonse woyambayamba.
19 Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa Iye chidzalo chonse chikhalire,
20 mwa Iyenso kuyanjanitsa zinthu zonse kwa Iye mwini, atachita mtendere mwa mwazi wa mtanda wake; mwa Iyetu, kapena za padziko, kapena za mu Mwamba.
21 Ndipo inu, okhala alendo kale ndi adani m’chifuwa chanu m’ntchito zoipazo,
22 koma tsopano anakuyanjanitsani m’thupi lake mwa imfayo, kukaimika inu oyera, ndi opanda chilema ndi osatsutsika pamaso pake;
23 ngatitu, mukhalabe m’chikhulupiriro, ochilimika ndi okhazikika ndi osasunthika kulekana nacho chiyembekezo cha Uthenga Wabwino umene mudaumva, wolalikidwa cholengedwa chonse cha pansi pa thambo; umene ine Paulo ndakhala mtumiki wake.
Machitachita a Paulo mu utumiki wake
24 Tsopano ndikondwera nazo zowawazo chifukwa cha inu, ndipo ndikwaniritsa zoperewera za chisautso cha Khristu m’thupi langa chifukwa cha thupi lake, ndilo Mpingowo;
25 amene ndinakhala mtumiki wake, monga mwa udindo wa Mulungu umene anandipatsa ine wakuchitira inu, wakukwaniritsa mau a Mulungu,
26 ndiwo chinsinsicho chinabisika kuyambira pa nthawizo, ndi kuyambira pa mibadwoyo; koma anachionetsa tsopano kwa oyera mtima ake,
27 kwa iwo amene Mulungu anafuna kuwazindikiritsa ichi chimene chili chuma cha ulemerero wa chinsinsi pakati paamitundu, ndiye Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero;
28 amene timlalikira ife, ndi kuchenjeza munthu aliyense ndi kuphunzitsa munthu aliyense mu nzeru zonse, kuti tionetsere munthu aliyense wamphumphu mwa Khristu;
29 kuchita ichi ndidzivutitsa ndi kuyesetsa monga mwa machitidwe ake akuchita mwa ine ndi mphamvu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/COL/1-af9ee1f2352534de984b6d2c0c2545e8.mp3?version_id=1068—