1 Mkuluyo kwa Gayo wokondedwayo, amene ndikondana naye m’choonadi.
2 Wokondedwa, ndipemphera kuti pa zonse ulemere, nukhale bwino, monga mzimu wako ulemera.
3 Pakuti ndinakondwera kwakukulu, pofika abale ndi kuchita umboni za choonadi chako, monga umayenda m’choonadi.
Za kuchereza abale ndi alendo
4 Ndilibe chimwemwe choposa ichi, chakuti ndimva za ana anga kuti alikuyenda m’choonadi.
5 Wokondedwa, uchita chokhulupirika nacho chilichonse, uwachitira abale ndi alendo omwe;
6 amene anachita umboni za chikondi chako pamaso paMpingo; ngati uwaperekeza amenewo pa ulendo wao koyenera Mulungu, udzachita bwino:
7 pakuti chifukwa cha dzinali anatuluka, osalandira kanthu kwaamitundu.
8 Chifukwa chake ife tiyenera kulandira otere, kuti tikakhale othandizana nacho choonadi.
Za Diotrefe ndi Demetrio
9 Ndalemba kanthu kwa Mpingo; komatu Diotrefe uja, wofuna kukhala wamkulu wa iwo, satilandira ife.
10 Momwemo, ndikadza ine, ndidzakumbutsa ntchito zake zimene achitazi, zakunena zopanda pake pa ife ndi mau oipa; ndipo popeza izi sizimkwanira, salandira abale iye yekha, ndipo ofuna kuwalandira awaletsa, nawataya kunja powatulutsa mu Mpingo.
11 Wokondedwa, usatsanza chili choipa komatu chimene chili chokoma. Iye wakuchita chokoma achokera kwa Mulungu; iye wakuchita choipa sanamuone Mulungu.
12 Demetrio, adamchitira umboni anthu onse, ndi choonadi chomwe; ndipo ifenso tichita umboni; ndipo udziwa kuti umboni wathu uli woona.
13 Ndinali nazo zambiri za kukulembera, komatu sindifuna kukulembera ndi kapezi ndi peni;
14 koma ndiyembekeza kukuona iwe msanga, ndipo tidzalankhula popenyana.
15 Mtendere ukhale nawe. Akupereka moni abwenzi. Upereke moni kwa abwenzi ndi kutchula maina ao.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/3JN/1-3ef7c2f35a82dd29d5c8d5893e907c93.mp3?version_id=1068—