Categories
2 AKORINTO

2 AKORINTO 10

Ulamuliro wa Paulo mtumwi

1 Koma ine ndekha Paulo, ndidandaulira inu mwa kufatsa ndi ulere waKhristu, ine amene pamaso panu ndikhala wodzichepetsa pakati pa inu, koma pokhala kwina ine ndilimbika mtima kwa inu;

2 koma ndipempha kuti pokhala ndili pomwepo, ndisalimbike mtima ndi kulimbika kumene ndiyesa kulimbika nako pa ena, amene atiyesera ife monga ngati tilikuyendayenda monga mwa thupi.

3 Pakuti pakuyendayenda m’thupi, sitichita nkhondo monga mwa thupi,

4 (pakuti zida za nkhondo yathu sizili za thupi, koma zamphamvu mwa Mulungu zakupasula malinga);

5 ndi kugwetsa matsutsano, ndi chokwezeka chonse chimene chidzikweza pokana chidziwitso cha Mulungu, ndi kugonjetsa ganizo lonse kukumvera kwa Khristu;

6 ndi kukhala okonzeka kubwezera chilango kusamvera konse, pamene kumvera kwanu kudzakwaniridwa.

7 Kodi mupenyera zopenyeka pamaso? Ngati wina alimbika mwa yekha kuti ali wa Khristu, ayesere ichinso mwa iye yekha, kuti monga iye ali wa Khristu, koteronso ife.

8 Pakuti ndingakhale ndikadzitamandira kanthu kochulukira za ulamuliro (umene anatipatsa Ambuye kukumangirira, ndipo si kukugwetsera kwanu), sindidzanyazitsidwa;

9 kuti ndisaoneke monga ngati kukuopsani mwa makalatawo.

10 Pakuti, makalatatu, ati, ndiwo olemera, ndi amphamvu; koma maonekedwe a thupi lake ngofooka, ndi mau ake ngachabe.

11 Woteroyo ayese ichi kuti monga tili ife ndi mau mwa makalata, pokhala palibe ife, tili oterenso m’machitidwe pokhala tili pomwepo.

12 Pakuti sitilimba mtima kudziwerenga, kapena kudzilinganiza tokha ndi ena a iwo amene adzivomeretsa okha; koma iwowa, podziyesera okha ndi iwo okha, ndi kudzilinganiza okha ndi iwo okha, alibe nzeru.

13 Koma ife sitidzadzitamandira popitirira muyeso, koma monga mwa muyeso wa chilekezero chimene Mulungu anatigawira muyeso, kufikira ngakhale kwa inunso.

14 Pakuti sitinyanyampiradi tokha, monga ngati sitinafikire kwa inu; pakuti tinadza kufikira inunso, mu Uthenga Wabwino wa Khristu:

15 osadzitamandira popitirira muyeso mwa machititso a ena; koma tili nacho chiyembekezo kuti pakukula chikhulupiriro chanu, tidzakulitsidwa mwa inu monga mwa chilekezero chathu kwa kuchulukira,

16 kukalalikira Uthenga Wabwino m’tsogolo mwake mwa inu, sikudzitamandira mwa chilekezero cha wina, ndi zinthu zokonzeka kale.

17 Koma iye wodzitamandira adzitamandire mwa Ambuye;

18 pakuti si iye amene adzitama yekha, koma iye amene Ambuye amtama ali wovomerezeka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CO/10-8cece938ecbeb348f6b313093016baac.mp3?version_id=1068—

Categories
2 AKORINTO

2 AKORINTO 11

Za atumwi onyenga

1 Bwenzi mutandilola pang’ono ndi chopusacho! Komanso mundilole.

2 Pakuti ndichita nsanje pa inu ndi nsanje ya Mulungu; pakuti ndinakupalitsani ubwenzi mwamuna mmodzi, kuti ndikalangize inu ngati namwali woyera mtima kwaKhristu.

3 Koma ndiopa, kuti pena, monga njoka inanyenga Heva ndi kuchenjerera kwake, maganizo anu angaipsidwe kusiyana nako kuona mtima ndi kuyera mtima zili kwa Khristu.

4 Pakutitu ngati iye wakudza alalikira Yesu wina, amene ife sitinalalikire, kapena ngati mulandira mzimu wa mtundu wina, umene simunalandire, kapena Uthenga Wabwino wa mtundu wina umene simunalandire, mulolana naye bwino lomwe.

5 Pakuti ndiyesa kuti sindinaperewere konse ndiatumwioposatu.

6 Ndipo ndingakhale ndili wosaphunzira m’manenedwe, koma sinditero m’chidziwitso, koma m’zonse tachionetsa kwa inu mwa anthu onse.

7 Kodi ndachimwa podzichepetsa ndekha, kuti inu mukakwezedwe, popeza ndinalalikira kwa inu Uthenga Wabwino wa Mulungu mwaufulu?

8 Ndinalanda zaMipingoina, ndi kulandira kwa iwo kulipira kuti ndikatumikire inu;

9 ndipo pakukhala nanu, ndi kusowa, sindinasaukitse munthu aliyense; pakuti abale akuchokera ku Masedoniya, anakwaniritsa kusowa kwanga; ndipo m’zonse ndinachenjera ndekha, ndisalemetse inu, ndipo ndidzachenjerapo.

10 Choonadi cha Khristu chili mwa ine, kuti kudzitamandira kumene sikudzaletsedwa kwa ine mu mbali zaAkaya.

11 Chifukwa ninji? Chifukwa sindikonda inu kodi? Adziwa Mulungu.

12 Koma chimene ndichita, ndidzachitanso, kuti ndikawadulire chifukwa iwo akufuna chifukwa; kuti m’mene adzitamandiramo, apezedwe monganso ife.

13 Pakuti otere ali atumwi onyenga, ochita ochenjerera, odzionetsa ngati atumwi a Khristu.

14 Ndipo kulibe kudabwa; pakutiSatanayemwe adzionetsa ngatimngelowa kuunika.

15 Chifukwa chake sikuli kanthu kwakukulu ngatinso atumiki ake adzionetsa monga atumiki a chilungamo; amene chimaliziro chao chidzakhala monga ntchito zao.

Kumva zowawa kwa Paulo chifukwa cha Uthenga Wabwino

16 Ndinenanso, Munthu asandiyese wopanda nzeru; koma ngati mutero, mundilandirenso ine monga wopanda nzeru, kuti inenso ndidzitamandire pang’ono.

17 Chimene ndilankhula sindilankhula monga mwa Ambuye, koma monga wopanda nzeru, m’kulimbika kumene kwa kudzitamandira.

18 Popeza ambiri adzitamandira monga mwa thupi, inenso ndidzadzitamandira.

19 Pakuti mulolana nao opanda nzeru mokondwera, pokhala anzeru inu nokha.

20 Pakuti mulola ngati wina akuyesani inu akapolo, ngati wina alikwira inu, ngati wina alanda zanu, ngati wina adzikuza, ngati wina akupandani pankhope.

21 Ndinena monga mwa kunyoza, monga ngati tinakhala ofooka. Koma m’mene wina alimbika mtimamo (ndinena mopanda nzeru) momwemo ndilimbika mtima inenso.

22 Kodi ali Ahebri? Inenso. Kodi ali Aisraele? Inenso. Kodi ali mbeu ya Abrahamu? Inenso.

23 Kodi ali atumiki a Khristu? (Ndilankhula monga moyaluka), makamaka ine; m’zivutinso mochulukira, m’ndende mochulukira, m’mikwingwirima mosawerengeka, muimfa kawirikawiri.

24 Kwa Ayuda ndinalandira kasanu mikwingwirima makumi anai kuperewera umodzi.

25 Katatu ndinamenyedwa ndi ndodo, kamodzi ndinaponyedwa miyala, katatu ndinatayika posweka chombo, ndinakhala m’kuya tsiku limodzi usana ndi usiku;

26 paulendo kawirikawiri, moopsa mwake mwa mitsinje, moopsa mwake mwa olanda, moopsa modzera kwa mtundu wanga, moopsa modzera kwaamitundu, moopsa m’mzinda, moopsa m’chipululu, moopsa m’nyanja, moopsa mwa abale onyenga;

27 m’chivutitso ndi m’cholemetsa, m’madikiro kawirikawiri, m’njala ndi ludzu, m’masalo a chakudya kawirikawiri, m’chisanu ndi umaliseche.

28 Popanda zakunjazo pali chondisindikiza tsiku ndi tsiku, chalabadiro cha Mipingo yonse.

29 Afooka ndani wosafooka inenso? Akhumudwitsidwa ndani, wosatenthanso ine?

30 Ngati ndiyenera kudzitamandira, ndidzadzitamandira ndi za kufooka kwanga.

31 Mulungu Atate wa Ambuye Yesu, Iye amene alemekezeka kunthawi yonse, adziwa kuti sindinama.

32 Mu Damasiko kazembe wa mfumu Areta analindizitsa mzinda wa Adamasiko kuti andigwire ine;

33 ndipo mwa zenera, mudengu, ananditsitsa pakhoma, ndipo ndinapulumuka m’manja mwake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CO/11-a3d287abbab31e12cc6d042b243ecbe5.mp3?version_id=1068—

Categories
2 AKORINTO

2 AKORINTO 12

Masomphenya a Paulo ndi munga m’thupi lake

1 Ndiyenera kudzitamandira, kungakhale sikupindulika; koma ndidzadza kumasomphenya ndi mavumbulutso a Ambuye.

2 Ndidziwa munthu wa mwaKhristu, zitapita zaka khumi ndi zinai (ngati m’thupi, sindidziwa; ngati kunja kwa thupi, sindidziwa; adziwa Mulungu), anakwatulidwa wotereyo kunka naye Kumwamba kwachitatu.

3 Ndipo ndidziwa munthu wotereyo (ngati m’thupi, ngati wopanda thupi, sindidziwa; adziwa Mulungu),

4 kuti anakwatulidwa kunka ku Paradaiso, namva maneno osatheka kuneneka, amene saloleka kwa munthu kulankhula.

5 Chifukwa cha wotereyo ndidzadzitamandira; koma chifukwa cha ine ndekha sindidzadzitamandira, koma m’zofooka zanga.

6 Pakuti ngati ndikafuna kudzitamandira, sindidzakhala wopanda nzeru; pakuti ndidzanena choonadi; koma ndileka, kuti wina angandiwerengere ine koposa kumene andiona ine, kapena amva za ine.

7 Ndipo kuti ndingakwezeke koposa, chifukwa cha ukulu woposa wa mavumbulutso, kunapatsidwa kwa ine munga m’thupi, ndiye mngelo waSatanakuti anditundudze, kuti ndingakwezeke koposa.

8 Za ichi ndinapemphera Ambuye katatu kuti chichoke kwa ine.

9 Ndipo ananena kwa ine, Chisomo changa chikukwanira; pakuti mphamvu yanga ithedwa mu ufooko. Chifukwa chake makamaka ndidzadzitamandira mokondweratu m’mafooko anga, kuti mphamvu ya Khristu ikhale pa ine.

10 Chifukwa chake ndisangalala m’mafooko, m’ziwawa, m’zikakamizo, m’mazunzo, m’zipsinjiko, chifukwa cha Khristu; pakuti pamene ndifooka, pamenepo ndili wamphamvu.

Kusadzikonda kwa Paulo

11 Ndakhala wopanda nzeru, mwandichititsa kutero; pakuti inu munayenera kundivomereza; pakuti sindiperewere ndiatumwioposatu m’kanthu konse, ndingakhale ndili chabe.

12 Zizindikirotu za mtumwi zinachitika pakati pa inu, m’chipiriro chonse, ndi zizindikiro, ndi zozizwa, ndi zamphamvu.

13 Pakuti kuli chiyani chimene munachepetsedwa nacho ndiMipingoyotsala ina, ngati si ichi kuti ine ndekha sindinasaukitse inu? Ndikhululukireni choipa ichi.

14 Taonani, nthawi yachitatu iyi ndapukwa ine kudza kwa inu, ndipo sindidzakusaukitsani; pakuti sindifuna zanu, koma inu; pakuti ana sayenera kuunjikira atate ndi amai, koma atate ndi amai kuunjikira ana.

15 Ndipo ndidzapereka ndi kuperekedwa konse chifukwa cha miyoyo yanu mokondweratu. Ngati ndikonda inu kochuluka koposa, kodi ndikondedwa kochepa?

16 Koma kukhale kotero; ine sindinalemetsa inu; koma pokhala wochenjera ine, ndinakugwirani ndi chinyengo.

17 Kodi wina wa iwo ndinawatuma kwa inu, ndinakuchenjererani naye kodi?

18 Ndinadandaulira Tito, ndipo ndinatuma mbaleyo naye. Kodi Tito anakuchenjererani kanthu? Sitinayendayende naye Mzimu yemweyo kodi? Sitinatsate mapazi omwewo kodi?

Malangizo otsiriza, zolawirana

19 Mumayesa tsopano lino kuti tilikuwiringula kwa inu. Tilankhula pamaso pa Mulungu mwa Khristu. Koma zonse, okondedwa, zili za kumangirira kwanu.

20 Pakuti ndiopa, kuti kaya, pakudza ine, sindidzakupezani inu otere onga ndifuna, ndipo ine ndidzapezedwa ndi inu wotere wonga simufuna; kuti kaya pangakhale chotetana, kaduka, mikwiyo, zilekanitso, maugogodi, ukazitape, zodzikuza, mapokoso;

21 kuti pakudzanso ine, Mulungu wanga angandichepse pa inu, ndipo ndingalirire ambiri a iwo amene adachimwa kale, osalapa pa chodetsa, ndi chigololo, ndi kukhumba zonyansa zimene anachita.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CO/12-344eb5cb7551bd612ac179b066d89567.mp3?version_id=1068—

Categories
2 AKORINTO

2 AKORINTO 13

1 Nthawi yachitatu iyi ndilinkudza kwa inu. Pakamwa pa mboni ziwiri kapena zitatu maneno onse adzakhazikika.

2 Ndinanena kale, ndipo ndinena ndisanafikeko, monga pamene ndinali pomwepo kachiwiri kaja, pokhala ine palibe, kwa iwo adachimwa kale ndi kwa onse otsala, kuti, ngati ndidzanso sindidzawaleka;

3 popeza mufuna chitsimikizo, chaKhristuwakulankhula mwa ine; amene safooka kwa inu, koma ali wamphamvu mwa inu;

4 pakuti anapachikidwa mu ufooko, koma ali ndi moyo mu mphamvu ya Mulungu. Pakuti ifenso tili ofooka mwa Iye, koma tidzakhala ndi moyo pamodzi ndi Iye, mu mphamvu ya Mulungu, ya kwa inu.

5 Dziyeseni nokha, ngati muli m’chikhulupiriro, dzitsimikizeni nokha. Kapena simuzindikira kodi za inu nokha kuti Yesu Khristu ali mwa inu? Mukapanda kukhala osatsimikizidwa.

6 Koma ndiyembekeza kuti mudzazindikira kuti sitili osatsimikizidwa.

7 Ndipo tipemphera Mulungu kuti musachite kanthu koipa; sikuti ife tikaoneke ovomerezeka, koma kuti inu mukachite chabwino, tingakhale ife tikhala monga osatsimikizidwa.

8 Pakuti sitikhoza kanthu pokana choonadi, koma povomereza choonadi.

9 Pakuti tikondwera, pamene ife tifooka ndi inu muli amphamvu; ichinso tipempherera, ndicho ungwiro wanu.

10 Chifukwa cha ichi ndilembera izi pokhala palibe ine, kuti pokhala ndili pomwepo ndingachite mowawitsa, monga mwa ulamuliro umene Ambuye anandipatsa ine wakumangirira, ndipo si wakugwetsa.

11 Chotsalira, abale, kondwerani. Muchitidwe angwiro; mutonthozedwe; khalani a mtima umodzi, khalani mumtendere; ndipo Mulungu wa chikondi ndi mtendere akhale pamodzi ndi inu.

12 Mupatsane moni ndi kupsompsonana kopatulika.

13 Oyera mtima onse akupatsani moni.

14 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mulungu, ndi chiyanjano cha Mzimu Woyera zikhale ndi inu nonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2CO/13-cafd3d8a2218b22ceeac103769253bb1.mp3?version_id=1068—