Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 10

Za imfa ya Saulo ndi ana ake

1 Afilisti tsono analimbana nkhondo ndi Israele; ndipo amuna a Israele anathawa pamaso pa Afilisti, nagwa ophedwa paphiri la Gilibowa.

2 Ndipo Afilisti anaumirira kutsata Saulo ndi ana ake, ndi Afilistiwo anapha Yonatani, ndi Abinadabu, ndi Malikisuwa, ana a Saulo.

3 Ndi nkhondoyi inamkulira Saulo, ndi amauta anampeza; ndipo anatenga nkhawa chifukwa cha amauta.

4 Pamenepo Saulo anati kwa wonyamula zida zake, Solola lupanga lako, nundipyoze nalo, angafike osadulidwa awa ndi kundiseka. Koma wonyamula zida zake anakana, popeza anaopa kwambiri. Pomwepo Saulo anatenga lupanga lake, naligwera.

5 Ndipo pamene wonyamula zida zake anaona kuti Saulo wafa, anagwera nayenso lupanga lake, nafa.

6 Momwemo anafa Saulo, ndi ana ake atatu; ndi nyumba yake yonse idafa pamodzi.

7 Ndipo pamene amuna onse a Israele okhala m’chigwamo anaona kuti anathawa, ndi kuti Saulo ndi ana ake adafa, anasiya mizinda yao, nathawa; nadza Afilisti, nakhala m’menemo.

8 Ndipo m’mawa mwake anafika Afilisti kuvula za ophedwa, napeza Saulo ndi ana ake adagwa paphiri la Gilibowa.

9 Ndipo anamvula natenga mutu wake, ndi zida zake, natumiza ku dziko la Afilisti pozungulirapo, kulalika m’mafano ao ndi mwa anthu.

10 Ndipo anaika zida zake m’nyumba ya milungu yao, napachika mutu wake m’nyumba ya Dagoni.

11 Ndipo onse a Yabesi-Giliyadi, atamva zonse Afilisti adachitira Saulo,

12 anauka ngwazi zonse, nachotsa mtembo wa Saulo, ndi mitembo ya ana ake, nabwera nayo ku Yabesi, naika mafupa ao patsinde pa mtengo wathundu ku Yabesi, nasala masiku asanu ndi awiri.

13 Momwemo Saulo anafa, chifukwa cha kulakwa kwake analakwira Yehova, kulakwira mau a Yehova amene sanawasunge; ndiponso chifukwa cha kufunsira wobwebweta, kufunsirako,

14 osafunsira kwa Yehova; chifukwa chake anamupha, napambutsira ufumu kwa Davide mwana wa Yese.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/10-ce37474650a18e5fe6c6cf04d4c913c0.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 11

Davide atalowa ufumu alanda Yerusalemu

1 Pamenepo Aisraele onse anasonkhana kwa Davide ku Hebroni, ndi kuti, Taonani, ife ndife fupa lanu, ndi mnofu wanu.

2 Ngakhale kale lomwe, pokhala mfumu Sauloyo, wotuluka ndi kulowa nao Aisraele ndinu; ndipo Yehova Mulungu wanu anati kwa inu, Uzidyetsa anthu anga Aisraele, nukhale mtsogoleri wa anthu anga Israele.

3 Akulu onse omwe a Israele anadza kwa mfumu ku Hebroni; ndipo Davide anapangana nao pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova; ndipo anamdzoza Davide akhale mfumu ya Israele monga mwa mau a Yehova, ndi dzanja la Samuele.

4 Namuka Davide ndi Aisraele onse naye kuYerusalemu, ndiwo Yebusi; ndipo Ayebusi nzika za m’dziko zinali komweko.

5 Ndipo nzika za mu Yebusi zinati kwa Davide, Sungalowe muno. Koma Davide analanda linga laZiyoni, ndiwo mzinda wa Davide.

6 Nati Davide, Aliyense woyamba kukantha Ayebusi, yemweyo adzakhala mkulu ndi mtsogoleri. Nayamba kukwerako Yowabu mwana wa Zeruya, nakhala mkulu iyeyu.

7 Ndipo Davide anakhala m’lingamo; chifukwa chake analitcha mzinda wa Davide.

8 Ndipo anamanga mzinda pozungulira pake, kuyambira ku Milo ndi pozungulira pake; ndi Yowabu anakonzanso potsala pa mzinda.

9 Ndipo Davide anakulakulabe, pakuti Yehova wa makamu anali naye.

Amphamvu a Davide

10 Akulu a amphamvu aja Davide anali nao akulimbika pamodzi naye mu ufumu wake, pamodzi ndi Aisraele onse, kumlonga ufumu, monga mwa mau a Yehova akunena za Israele, ndi awa.

11 Kuwerenga kwa amphamvu aja Davide anali nao ndi uku: Yasobeamu mwana wa Muhakimoni, mkulu wa makumi atatu aja, anasamulira mazana atatu mkondo wake, nawapha nthawi imodzi.

12 Ndi pambuyo pake Eleazara mwana wa Dodo Mwahohi, ndiye mmodzi wa atatu aja amphamvu.

13 Anali pamodzi ndi Davide ku Pasidamimu muja; Afilisti anasonkhanako kunkhondo kumene kunali munda wodzala ndi barele; ndipo anthu anathawa pamaso pa Afilisti.

14 Koma anadziimika pakati pamunda, naulanditsa, nakantha Afilisti; m’mwemo anawapulumutsa Yehova ndi chipulumutso chachikulu.

15 Ndipo atatu a akulu makumi atatu anatsikira kuthanthwe kwa Davide, ku phanga la Adulamu; ndi nkhondo ya Afilisti idamanga misasa m’chigwa cha Refaimu.

16 Pamenepo Davide anali m’linga, ndi boma la asilikali a Afilisti linali ku Betelehemu.

17 Ndipo Davide analakalaka, nati, Ha? Mwenzi wina atandimwetsa madzi a m’chitsime cha ku Betelehemu chili kuchipata.

18 Napyola atatuwo misasa ya Afilisti natunga madzi ku chitsime cha ku Betelehemu chili kuchipata, nabwera nao kwa Davide; koma Davide anakana kumwako, koma anawathirira kwa Yehova;

19 nati, Pali Mulungu wanga, kukhale kutali kwa ine kuchita ichi. Ngati ndidzamwa mwazi wa anthu awa? Akadataya moyo wao, inde akadataya moyo wao, pakukatenga madziwa. M’mwemo sanafune kuwamwa. Izi anazichita atatu amphamvuwa.

20 Ndipo Abisai mbale wa Yowabu, ndiye wamkulu wa atatuwa; pakuti anasamulira mazana atatu mkondo wake, nawapha, namveka dzina pakati pa atatuwa.

21 Mwa atatuwa iye anali waulemu woposa awiriwa, nasanduka mkulu wao; koma sanafike pa atatu oyamba aja.

22 Benaya mwana wa Yehoyada, mwana wa ngwazi ya ku Kabizeeli, wochita zachikulu, anapha ana awiri a Ariyele wa ku Mowabu; anatsikanso, napha mkango m’kati mwa dzenje nyengo ya chipale chofewa.

23 Anaphanso Mwejipito munthu wamkulu, msinkhu wake mikono isanu, ndi m’dzanja la Mwejipito munali mkondo ngati mtanda woombera nsalu; ndipo anamtsikira ndi ndodo, nakwatula mkondo m’dzanja la Mwejipito, namupha ndi mkondo wake womwe.

24 Izi anazichita Benaya mwana wa Yehoyada, namveka dzina mwa atatu amphamvuwo.

25 Taonani, anali wa ulemu woposa makumi atatuwo, koma sanafike pa atatu oyamba aja; ndipo Davide anamuika mkulu wa olindirira ake.

26 Ndipo amphamvuwo a magulu a nkhondo ndiwo Asahele mbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,

27 Samoti Muharodi, Helezi Mpeloni,

28 Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa, Abiyezere wa ku Anatoti,

29 Sibekai Muhusa, Ilai Mwahohi,

30 Maharai Mnetofa, Heledi mwana wa Baana Mnetofa,

31 Itai mwana wa Ribai wa Gibea wa ana a Benjamini, Benaya Mpiratoni,

32 Hurai wa ku mitsinje ya Gaasi, Abiyele Mwarabati,

33 Azimaveti Mbaharumi, Eliyaba Msaaliboni;

34 ana a Hasemu Mgizoni; Yonatani mwana wa Sage Muharari,

35 Ahiyamu mwana wa Sakara Muharari, Elifala mwana wa Uri,

36 Hefere Mmekerati, Ahiya Mpeloni,

37 Heziro wa ku Karimele, Naarai mwana wa Ezibai,

38 Yowele mbale wa Natani, Mibara mwana wa Hagiri,

39 Zeleki Mwamoni, Naharai Mbeeroti wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,

40 Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,

41 Uriya Muhiti, Zabadi mwana wa Alai,

42 Adina mwana wa Siza Mrubeni mkulu wa Arubeni, ndi makumi atatu pamodzi naye,

43 Hanani mwana wa Maaka, ndi Yosafati Mmitini,

44 Uziya Mwasiterati, Sama ndi Yeiyele ana a Hotamu wa ku Aroere,

45 Yediyaele mwana wa Simiri, ndi Yoha mbale wake Mtizi,

46 Eliyele Mmahavi, ndi Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu, ndi Itima Mmowabu,

47 Eliyele, ndi Obedi, ndi Yaasiyele Mmezobai.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/11-d7479049efe045195a7d123a5b7b1d93.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 12

Amphamvu anadza kwa Davide namtsata pomlonda Saulo

1 Anadzawo kwa Davide ku Zikilagi, akali chitsekedwere chifukwa cha Saulo mwana wa Kisi, ndi awa; ndiwo mwa amphamvuwo omthandiza kunkhondo.

2 Anakoka mauta; naponya miyala, naponya mivi ndi uta ndi dzanja lamanja ndi lamanzere lomwe; ndiwo a abale ake a Saulo, Abenjamini.

3 Mkulu wao ndiye Ahiyezere, ndi Yowasi, ana a Semaa wa ku Gibea; ndi Yeziyele, ndi Peleti, ana a Azimaveti; ndi Beraka, ndi Yehu wa ku Anatoti,

4 ndi Isimaya wa ku Gibiyoni, wamphamvu mwa makumi atatuwo ndi woyang’anira makumi atatuwo, ndi Yeremiya, ndi Yahaziele, ndi Yohanani, ndi Yozabadi wa ku Gedera,

5 Eluzai, ndi Yerimoti, ndi Bealiya, ndi Semariya, ndi Sefatiya wa ku Harufi,

6 Elikana, ndi Isiya, ndi Azarele, ndi Yowezere, ndi Yasobeamu ndiwo Akora;

7 ndi Yowela, ndi Zebadiya, ana a Yerohamu wa ku Gedori.

8 Ndi Agadi ena anapatukira kwa Davide ku linga la m’chipululu, ngwazi zamphamvu zozerewera nkhondo, zogwira chikopa ndi mkondo; nkhope zao zikunga nkhope za mikango, ndi liwiro lao longa la ngoma mumapiri:

9 Ezere mkulu wao, wachiwiri Obadiya, wachitatu Eliyabu,

10 wachinai Misimana, wachisanu Yeremiya,

11 wachisanu ndi chimodzi Atai, wachisanu ndi chiwiri Eliyele,

12 wachisanu ndi chitatu Yohanani, wachisanu ndi chinai Elizabadi,

13 wakhumi Yeremiya, wakhumi ndi chimodzi Makibanai.

14 Awa a ana a Gadi, anali atsogoleri a nkhondo; wamng’ono wa iwo anayang’anira zana limodzi, ndi wamkulu wa iwo anayang’anira chikwi chimodzi.

15 Awa ndi omwe aja anaoloka Yordani mwezi woyamba, atadzala kusefukira magombe ake onse; nathawitsa onse okhala m’zigwa kum’mawa ndi kumadzulo.

16 Ndipo anadza ena a ana a Benjamini ndi Yuda kulinga kwa Davide.

17 Ndipo Davide anatuluka kukomana nao, nayankha, nanena nao, Ngati mwandidzera mwamtendere kundithandiza, mtima wanga udzalumikizana nanu; koma ngati mwafika kundipereka kwa adani anga, popeza m’manja mwanga mulibe chiwawa, Mulungu wa makolo athu achione ndi kuchilanga.

18 Pamenepo mzimu unavala Amasai, ndiye wamkulu wa makumi atatuwo, nati iye, Ndife anu, Davide, tivomerezana nanu mwana wa Yese inu: mtendere, mtendere ukhale ndi inu, ndi mtendere ukhale ndi athandizi anu; pakuti Mulungu wanu akuthandizani. Ndipo Davide anawalandira, nawaika akulu a magulu.

19 Ena a Manase omwe anapatukira kwa Davide, muja iye anadza ndi Afilisti koponyana nkhondo ndi Saulo, koma sanawathandize; popeza akalonga a Afilisti, atachita upo, anamuuza achoke, ndi kuti, Adzapatukira kwa mbuye wake Saulo ndi kutisandulikira.

20 Pomuka iye ku Zikilagi anapatukira kwa iye a Manase: Adina, ndi Yozabadi, ndi Yediyaele, ndi Mikaele, ndi Yozabadi, ndi Elihu, ndi Ziletai, akulu a zikwi a ku Manase.

21 Ndipo anathandiza Davide aponyane nalo gulu la achifwamba, pakuti onse ndiwo ngwazi zamphamvu, nakhala atsogoleri m’khamu la nkhondo.

22 Pakuti nthawi yomweyo anadza kwa Davide kumthandiza, mpaka kunali nkhondo yaikulu, ngati nkhondo ya Mulungu.

Akulu omponya Davide mfumu ku Hebroni

23 Ndipo kuwerenga kwa akulu okonzekeratu kunkhondo, anadzawo kwa Davide ku Hebroni, kupambukitsa ufumu wa Saulo ukhale wake, monga mwa mau a Yehova, ndi uku.

24 Ana a Yuda akunyamula zikopa ndi mikondo ndiwo zikwi zisanu ndi chimodzi mphambu mazana asanu ndi atatu, okonzekeratu kunkhondo.

25 A ana a Simeoni ngwazi zamphamvu za nkhondo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu zana limodzi.

26 A ana a Levi zikwi zinai mphambu mazana asanu ndi limodzi.

27 Ndipo Yehoyada, ndiye mtsogoleri wa nyumba ya Aroni, ndi pamodzi naye zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi awiri;

28 ndi Zadoki, ndiye mnyamata, ngwazi yamphamvu, ndi a nyumba ya kholo lake akulu makumi awiri mphambu awiri.

29 Ndi a ana a Benjamini, abale a Saulo, zikwi zitatu; pakuti mpaka pomwepo ochuluka a iwowa anaumirira nyumba ya Saulo.

30 Ndi a ana a Efuremu zikwi makumi awiri mphambu mazana asanu ndi atatu, ngwazi zamphamvu, anthu omveka m’nyumba za makolo ao.

31 Ndipo a hafu la fuko la Manase zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu, otchulidwa maina ao kuti adzalonge Davide mfumu.

32 Ndi a ana a Isakara, anthu akuzindikira nyengo, akudziwa zoyenera Israele kuzichita, akulu ao ndiwo mazana awiri; ndi abale ao onse anapenyerera pakamwa pao.

33 A Zebuloni akutuluka kukhamu, opangira nkhondo, monga mwa zida zilizonse za nkhondo, zikwi makumi asanu, akusunga malongosoledwe a nkhondo ndi mtima wosatekeseka.

34 Ndi a Nafutali atsogoleri chikwi chimodzi, ndi pamodzi nao ogwira zikopa ndi mikondo zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi ziwiri.

35 Ndi a Adani akupangira nkhondo zikwi makumi awiri mphambu zisanu ndi zitatu kudza mazana asanu ndi limodzi.

36 Ndi a Asere akutuluka kukhamu, akupangira nkhondo, zikwi makumi anai.

37 Ndi tsidya lija la Yordani a Arubeni, ndi Agadi, ndi hafu la fuko la Manase, ndi zina zilizonse za khamu kuchita nazo nkhondo, zikwi zana limodzi ndi makumi awiri.

38 Onsewa, ndiwo anthu a nkhondo akusunga malongosoledwe a nkhondo, anadza ku Hebroni ndi mtima wangwiro kudzamlonga Davide mfumu ya Aisraele onse; ndi onse otsala a Israele omwe anali a mtima umodzi kumlonga Davide ufumu.

39 Ndipo anali komweko kwa Davide masiku atatu kudya ndi kumwa, popeza abale ao anazikonzeratu.

40 Ndiponso akuyandikizana nao mpaka Isakara ndi Zebuloni ndi Nafutali anabwera nao mkate osenzetsa abulu, ndingamira, ndi nyuru, ndi ng’ombe, zakudya zaufa, ndi nchinchi zankhuyu, ndi nchinchi zamphesa, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi ng’ombe, ndi nkhosa zochuluka; pakuti munali chimwemwe mu Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/12-6ab6b68754b9bfc0714a8d9390c826e2.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 13

Apita nalo likasa nalisunga m’nyumba ya Obededomu

1 Ndipo Davide anafunsana ndi akulu a zikwi ndi a mazana, inde atsogoleri ali onse.

2 Ndipo Davide anati kwa msonkhano wonse wa Israele, Chikakomera inu, ndipo chikachokera kwa Yehova Mulungu wathu, titumize konse kuti abale athu otsala m’dziko lonse la Israele, ndi ansembe ndi Alevi okhala nao m’mizinda yao yokhala napo podyetsa, kuti asonkhane kwa ife;

3 ndipo tibwere nalo kwa ife likasa la Mulungu wathu, pakuti sitinafunako masiku a Saulo.

4 Ndipo a msonkhano onse anati kuti adzachita; pakuti chidayenera chinthuchi pamaso pa anthu onse.

5 M’mwemo Davide anamemeza Aisraele onse kuyambira Sihori wa ku Ejipito mpaka polowera ku Hamati, kutenga likasa la Mulungu ku Kiriyati-Yearimu.

6 Ndipo Davide ndi Aisraele onse pamodzi naye anakwera kunka ku Baala, ndiko ku Kiriyati-Yearimu wa mu Yuda, kukwera nalo kuchokera komweko likasa la Mulungu Yehova wakukhala paakerubi, kumene aitanirako Dzina.

7 Ndipo anatengera likasa la Mulungu pa galeta watsopano kuchokera kunyumba ya Abinadabu; ndi Uza ndi Ahiyo anayendetsa ng’ombe za pa galetayo.

8 Ndipo Davide ndi Aisraele onse anasewera pamaso pa Mulungu ndi mphamvu yao yonse; ndi nyimbo, ndi azeze, ndi zisakasa, ndi malingaka, ndi nsanje, ndi malipenga.

9 Ndipo pamene anafika ku dwale la Kidoni, Uza anatambasula dzanja lake kulichirikiza likasa, pakuti ng’ombe zikadapulumuka.

10 Ndi mkwiyo wa Yehova unayakira Uza, namkantha, chifukwa anatambasulira likasa dzanja lake, nafa komweko pamaso pa Mulungu.

11 Ndipo kudaipira Davide kuti Yehova adachita chipasulo ndi Uza; motero anatcha malowo Pereziuza, mpaka lero lino.

12 Ndipo Davide anaopa Mulungu tsikulo, kuti, Ndidzafika nalo bwanji likasa la Mulungu kwathu?

13 M’mwemo Davide sanafike nalo likasa kwao kumzinda wa Davide, koma analipambutsira kunyumba ya Obededomu wa ku Giti.

14 Ndi likasa la Mulungu linakhala ndi banja la Obededomu m’nyumba mwake miyezi itatu; ndipo Yehova anadalitsa nyumba ya Obededomu, ndi zonse anali nazo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/13-203a15a2bc261ddf1c306801e1b138fd.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 14

Chibwenzi cha Hiramu, kulephera kwa Afilisti

1 Ndipo Huramu mfumu ya Tiro anatumiza mithenga kwa Davide, ndi mikungudza, ndi amisiri omanga miyala, ndi amatabwa, kuti ammangire nyumba.

2 Ndipo Davide anazindikira kuti Yehova adamkhazikitsa mfumu ya Israele; pakuti ufumu wake unakwezekadi, chifukwa cha anthu ake Israele.

3 Ndipo Davide anatenga akazi ena ku Yerusalemu, nabala Davide ana aamuna ndi aakazi ena.

4 Maina a ana anali nao mu Yerusalemu ndi awa: Samuwa, ndi Sobabu Natani, ndi Solomoni,

5 ndi Ibara, ndi Elisuwa, ndi Elipeleti,

6 ndi Noga, ndi Nefegi, ndi Yafiya,

7 ndi Elisama, ndi Beeliyada, ndi Elifeleti.

8 Pamene Afilisti anamva kuti anamdzoza Davide akhale mfumu ya Aisraele onse, Afilisti onse anakwera kufunafuna Davide; ndipo Davide anamva, nawatulukira.

9 Afilisti tsono anafika, nafalikira m’chigwa cha Refaimu.

10 Ndipo Davide anafunsira kwa Mulungu, kuti, Ndikwere kodi kuyambana ndi Afilisti? Mudzawapereka m’dzanja langa kodi? Ndipo Yehova anati kwa iye, Kwera, pakuti ndidzawapereka m’dzanja lako.

11 Atafika tsono ku Baala-Perazimu, Davide anawakantha komweko; nati Davide, Mulungu anapasula adani anga ndi dzanja langa, ngati pokhamulira madzi. Chifukwa chake analitcha dzina la malowo Baala-Perazimu.

12 Ndipo anasiyako milungu yao; nalamula Davide, ndipo anaitentha ndi moto.

13 Ndipo Afilisti anabwerezanso, nafalikira m’chigwamo.

14 Ndipo Davide anafunsiranso kwa Mulungu, nanena Mulungu naye, Usakwera kuwatsata, uwazungulire, nuwadzere pandunji pa mitengo ya mkandankhuku.

15 Ndipo kudzali, pakumva iwe kuwayula kunsonga kwa mitengo ya mkandankhuku, pamenepo utulukire kunkhondo; pakuti Mulungu watulukira pamaso pako kukantha gulu la Afilisti.

16 Nachita Davide monga Mulungu adamuuza, nakantha gulu la Afilisti kuyambira ku Gibiyoni kufikira ku Gezere.

17 Ndipo mbiri ya Davide inabuka m’maiko onse, nafikitsira Yehova kuopsa kwake pa amitundu onse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/14-44f928780734f39fe975c033601f550e.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 15

Davide afikitsa likasa ku Yerusalemu, nalongosola mapembedzedwe

1 Ndipo Davide anadzimangira nyumba m’mzinda mwake, nakonzeratu malo likasa la Mulungu, naliutsira hema.

2 Pamenepo Davide anati, Sayenera ena kusenza likasa la Mulungu koma Alevi ndiwo; pakuti Yehova anawasankha iwo kusenza likasa la Mulungu, ndi kumtumikira Iye kosatha.

3 Ndipo Davide anasonkhanitsira Aisraele onse kuYerusalemu, akwere nalo likasa la Yehova kumalo kwake adalikonzera.

4 Ndipo Davide anasonkhanitsa ana a Aroni ndi Alevi;

5 a ana a Kohati, Uriyele mkulu wao, ndi abale ake zana limodzi mphambu makumi awiri;

6 a ana a Merari, Asaya mkulu wao, ndi abale ake mazana awiri mphambu makumi awiri;

7 a ana a Geresomo, Yowele mkulu wao, ndi abale ake zana limodzi mphambu makumi atatu;

8 a ana a Elizafani, Semaya mkulu wao, ndi abale ake mazana awiri;

9 a ana a Hebroni, Eliyele mkulu wao, ndi abale ake makumi asanu ndi atatu;

10 a ana a Uziyele, Aminadabu mkulu wao, ndi abale ake zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.

11 Ndipo Davide anaitana Zadoki ndi Abiyatara ansembe, ndi Alevi Uriyele, Asaya, ndi Yowele, Semaya, ndi Eliyele, ndi Aminadabu, nanena nao,

12 Inu ndinu akulu a nyumba za makolo a Alevi, mudzipatule inu ndi abale anu omwe, kuti mukatenge ndi kukwera nalo likasa la Yehova Mulungu wa Israele ku malo ndalikonzera.

13 Pakuti, chifukwa cha kusalinyamula inu poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anachita chotipasula, popeza sitinamfunafuna Iye monga mwa chiweruzo.

14 Momwemo ansembe ndi Alevi anadzipatula kuti akwere nalo likasa la Yehova Mulungu wa Israele.

15 Ndipo ana a Alevi anasenza likasa la Mulungu pa mapewa ao, mphiko zili m’mwemo, monga Mose anawauza, monga mwa mau a Yehova.

16 Ndipo Davide ananena ndi mkulu wa Alevi kuti aike abale ao oimbawo ndi zoimbira, zisakasa, ndi azeze, ndi nsanje, azimveketse ndi kukweza mau ao ndi chimwemwe.

17 Ndipo Alevi anaika Hemani mwana wa Yowele, ndi a abale ake Asafu mwana wa Berekiya, ndi a ana a Merari, abale ao, Etani mwana wa Kusaya;

18 ndi pamodzi nao abale ao a kulongosola kwachiwiri, Zekariya, Beni, ndi Yaaziele, ndi Semiramoti, ndi Yehiyele, ndi Uni, Eliyabu, ndi Benaya, ndi Maaseiya, ndi Matitiya, ndi Elifelehu, ndi Mikineya, ndi Obededomu, ndi Yeiyele, odikirawo.

19 Oimba tsono: Hemani, Asafu, ndi Etani, anaimba ndi nsanje zamkuwa;

20 ndi Zekariya, ndi Aziyele, ndi Semiramoti, ndi Yehiyele, ndi Uni, ndi Eliyabu, ndi Maaseiya, ndi Benaya, ndi zisakasa kuimbira mwa Alimoti;

21 ndi Matitiya, ndi Elifelehu, ndi Mikineya, ndi Obededomu, ndi Yeiyele, ndi Azaziya, ndi azeze akuimbira mwa Seminiti, kutsogolera maimbidwe.

22 Ndi Kenaniya mkulu wa Alevi anayang’anira kusenzako; anawalangiza za kusenza, pakuti anali waluso.

23 Ndi Berekiya ndi Elikana anali odikira likasa.

24 Ndi Sebaniya, ndi Yosafati, ndi Netanele, ndi Amasai, ndi Zekariya, ndi Benaya, ndi Eliyezere, ansembe, analiza malipenga ku likasa la Mulungu; ndi Obededomu ndi Yehiya anali odikira a likasa.

25 Momwemo Davide, ndi akuluakulu a Israele, ndi atsogoleri a zikwi, anamuka kukwera nalolikasa la chipanganola Yehova, kuchokera kunyumba ya Obededomu mokondwera.

26 Ndipo popeza Mulungu anathandiza Alevi akusenza likasa la chipangano la Yehova, iwo anapha nsembe ng’ombe zisanu ndi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri.

27 Ndipo Davide anavala malaya abafuta, ndi Alevi onse akunyamula likasa, ndi oimba, ndi Kenaniya woyang’anira kusenzaku, pamodzi ndi oimba; Davide anavalansoefodiwabafuta.

28 Momwemo Aisraele onse anakwera nalo likasa la chipangano la Yehova ndi kufuula, ndi kumveka kwa lipenga, ndi mphalasa, ndi nsanje zomveketsa, ndi zisakasa, ndi azeze.

29 Ndipo polowa likasa la chipangano la Yehova m’mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Saulo anasuzumira pazenera, nao mfumu Davide alikutumphatumpha ndi kusewera; ndipo anampeputsa mumtima mwake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/15-4fc5b1d334d188b50f668fb001b15796.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 16

1 Ndipo analowa nalo likasa la Mulungu, naliika pakati pa hemalo Davide adaliutsira; ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zoyamika pamaso pa Mulungu.

2 Ndipo atatha Davide kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zoyamika, anadalitsa anthu m’dzina la Yehova.

3 Nagwira aliyense wa Israele, wamwamuna ndi wamkazi, yense mtanda wa mkate, ndi nthuli ya nyama, ndi nchinchi ya mphesa zouma.

4 Ndipo anaika Alevi ena atumikire ku likasa la Yehova, nalalikire, nayamike, nalemekeze Yehova Mulungu wa Israele.

5 Asafu ndiye mkulu wao, ndi otsatana naye Zekariya, Yeiyele, ndi Semiramoti, ndi Yehiyele, ndi Matitiya, ndi Eliyabu, ndi Benaya, ndi Obededomu, ndi Yeiyele, ndi zisakasa ndi azeze; koma Asafu ndi nsanje zomvekatu;

6 ndi Benaya ndi Yahaziele ansembe ndi malipenga kosalekeza, kulikasa la chipanganola Mulungu.

Salimo la Davide

7 Tsiku limenelo tsono Davide anayamba kuwapatsa nyimbo ya kuyamika nayo Yehova; ochita ndiwo Asafu ndi abale ake.

8 Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

bukitsani mwa mitundu ya anthu zochita Iye.

9 Muimbireni, muimbireni zomlemekeza;

fotokozerani zodabwitsa zake zonse.

10 Mudzitamandire ndi dzina lake lopatulika;

mitima yao ya iwo ofuna Yehova ikondwere.

11 Funsirani kwa Yehova ndi mphamvu yake;

funani nkhope yake nthawi zonse.

12 Kumbukirani zodabwitsa zake adazichita,

zizindikiro zake, ndi maweruzo a pakamwa pake.

13 Inu mbeu ya Israele mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhika ake.

14 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

maweruzo ake akhala padziko lonse lapansi.

15 Kumbukirani chipangano chake kosatha,

mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

16 chipanganocho anapangana ndi Abrahamu,

ndi lumbiro lake ndi Isaki;

17 ndipo anachitsimikizira kwa Yakobo chikhale malemba,

chikhale chipangano chosatha kwa Israele;

18 ndi kunena kuti,

Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,

gawo la cholowa chako.

19 Pokhala inu anthu owerengeka,

inde anthu pang’ono, ndi alendo m’mwemo;

20 nayendayenda kuchokera mtundu wina kufikira mtundu wina,

kuchokera ufumu wina kufikira anthu ena.

21 Sanalole munthu awasautse;

ndipo anadzudzula mafumu chifukwa cha iwowa;

22 ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga,

musamachitira choipa aneneri anga.

23 Muimbireni Yehova, inu dziko lonse lapansi,

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

24 Fotokozerani ulemerero wake mwa amitundu,

zodabwitsa zake mwa mitundu yonse ya anthu.

25 Pakuti Yehova ali wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;

ayenera amuope koposa milungu yonse.

26 Pakuti milungu ya mitundu ya anthu ndiyo mafano;

koma Yehova analenga zakumwamba.

27 Pamaso pake pali ulemu ndi ukulu,

m’malo mwake muli mphamvu ndi chimwemwe.

28 Mchitireni Yehova, inu mafuko a mitundu ya anthu,

mchitireni Yehova ulemerero ndi mphamvu.

29 Mchitireni Yehova ulemerero wa dzina lake;

bwerani nacho chopereka, ndipo fikani pamaso pake;

lambirani Yehova m’chiyero chokometsetsa.

30 Njenjemerani pamaso pake, inu dziko lonse lapansi,

dziko lokhalamo anthu lomwe lakhazikika, kuti silingagwedezeke.

31 Kukondwerere kumwamba, ndi dziko lapansi lisekerere;

anene mwa amitundu, Yehova achita ufumu.

32 Nyanja ikukume m’kudzala kwake,

munda ukondwerere, ndi zonse zili m’mwemo.

33 Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango

idzafuula mokondwera pamaso pa Yehova;

pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi.

34 Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino;

pakuti chifundo chake nchosatha.

35 Nimunene, Tipulumutseni,

Mulungu wa chipulumutso chathu;

mutisokolotse ndi kutilanditsa kwaamitundu,

kuti tiyamike dzina lanu loyera,

ndi kudzitamandira nacho chilemekezo chanu.

36 Alemekezedwe Yehova Mulungu wa Israele,

kuyambira kosayamba kufikira kosatha.

Ndipo anthu onse anati, Amen! Nalemekeza Yehova.

37 Ndipo anasiyako ku likasa la chipangano la Yehova Asafu ndi abale ake, atumikire kulikasa kosalekeza, monga umo mudzafunika tsiku ndi tsiku;

38 ndi Obededomu, ndi abale ake makumi asanu ndi limodzi mphambu asanu ndi atatu; ndi Obededomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa akhale odikira;

39 ndi Zadoki wansembe, ndi abale ake ansembe, ku chihema cha Yehova, pa msanje unali ku Gibiyoni;

40 kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova paguwa la nsembe zopsereza, kosalekeza, m’mawa ndi madzulo, monga mwa zonse zilembedwa m’chilamulo cha Yehova adachilamulira Israele;

41 ndi pamodzi nao Hemani, ndi Yedutuni, ndi osankhika otsalawo, otchulidwa maina, kuyamika Yehova; pakuti chifundo chake nchosatha;

42 ndi pamodzi nao Hemani, ndi Yedutuni, ndi malipenga ndi nsanje za iwo akumveketsadi, ndi zoimbira nyimbo za Mulungu; ndi ana a Yedutuni anakhala kuchipata.

43 Ndipo anachoka anthu onse, yense kunyumba yake, nabwera Davide kudalitsa nyumba yake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/16-a516b991ed143e460b336de6737dc9fa.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 17

Yehova salola Davide ammangire Kachisi

1 Ndipo pokhala Davide m’nyumba mwake, Davideyo anati kwa Natanimneneri, Taona, ndikhala ine m’nyumba yamikungudza, komalikasa la chipanganola Yehova likhala m’nsalu zotchinga.

2 Ndipo Natani anati kwa Davide, Muchite zonse zili m’mtima mwanu; pakuti Mulungu ali nanu.

3 Ndipo usiku womwewo mau a Mulungu anadzera Natani, ndi kuti,

4 Kauze Davide mtumiki wanga, Atero Yehova, Usandimangire nyumba yokhalamo;

5 pakuti sindinakhale m’nyumba kuyambira tsiku lija ndinakwera naye Israele, kufikira lero lino; koma ndakhala ndikuyenda m’mahema uku ndi uku.

6 Pali ponse ndinayenda nao Aisraele onse ndinanena kodi mau ndi woweruza aliyense wa Israele, amene ndinamuuza adyetse anthu anga, ndi kuti, Mwalekeranji kundimangira nyumba yamikungudza?

7 Chifukwa chake tsono, uzitero naye mtumiki wanga Davide, Atero Yehova wa makamu, Ndinakutenga kubusa potsata iwe nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Israele;

8 ndipo ndakhala ndi iwe kulikonse unamukako, ndi kuononga adani ako onse pamaso pako; ndipo ndakubukitsira dzina lakunga dzina la akulu okhala padziko.

9 Ndipo ndaikira anthu anga Israele malo, ndi kuwaoka, kuti akhale m’malo mwao osasunthikanso; ndi ana osalungama sadzawapululanso monga poyamba paja;

10 ndi kuyambira kuja ndinaika oweruza ayang’anire anthu anga Israele; ndipo ndagonjetsa adani ako onse. Ndikuuzanso kuti Yehova adzakumangira banja.

11 Ndipo kudzachitika, atakwanira masiku ako kuti uzipita kukhala ndi makolo ako, ndidzaukitsa mbeu yako pambuyo pako, ndiye wa ana ako; ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.

12 Iye adzandimangira nyumba; ndipo ndidzakhazikitsa mpando wachifumu wake kosatha.

13 Ndidzakhala atate wake, ndi iye adzakhala mwana wanga; ndipo sindidzamchotsera chifundo changa monga muja ndinachotsera iye amene anakhala usanakhale iwe;

14 koma ndidzamkhazikitsa m’nyumba mwanga, ndi mu ufumu wanga kosatha; ndi mpando wachifumu wake udzakhazikika kosatha.

15 Monga mwa mau awa onse, ndi monga mwa masomphenya awa onse, momwemo Natani analankhula ndi Davide.

Chonena Davide

16 Pamenepo mfumu Davide analowa nakhala pamaso pa Yehova, nati, Ndine yani, Yehova Mulungu, ndi nyumba yanga njotani kuti mwandifikitsa mpaka pano?

17 Ndipo ichi nchaching’ono pamaso panu, Mulungu, koma mwanena za nyumba ya mtumiki wanu nthawi yam’tsogolo ndithu, ndipo mwandiyesera ngati munthu womveka, Yehova Mulungu.

18 Anenenjinso Davide kwa inu za ulemu wochitikira mtumiki wanu? Pakuti mudziwa mtumiki wanu.

19 Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu, ndi monga mwa mtima wanu, mwachita ukulu uwu wonse, kundidziwitsa zazikulu izi zonse.

20 Yehova, palibe wina wonga inu, palibenso Mulungu wina koma Inu; monga mwa zonse tazimva m’makutu mwathu.

21 Ndiwo ayani akunga anthu anu Israele, mtundu wa pa wokha wa padziko lapansi, amene Mulungu anakadziombolera mtundu wa anthu, kudzibukitsira dzina, mwa zazikulu ndi zoopsa, pakupirikitsaamitundupamaso pa anthu anu amene munawaombola mu Ejipito?

22 Pakuti anthu anu Israele mudawayesa anthu anuanu kosatha; ndipo Inu, Yehova, munayamba kukhala Mulungu wao.

23 Ndipo tsopano, Yehova, akhazikike kosalekeza mau mudanenawa za mtumiki wanu, ndi za nyumba yake, nimuchite monga mwanena.

24 Inde likhazikike dzina lanu, likulitsidwe kosalekeza, ndi kuti, Yehova wa makamu ndiye Mulungu wa Israele; akhalira Israele Mulungu; ndi nyumba ya Davide mtumiki wanu ikhazikika pamaso panu.

25 Pakuti Inu, Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzammangira banja; momwemo mtumiki wanu waona mtima wakupemphera pamaso panu.

26 Ndipo tsopano, Yehova, Inu ndinu Mulungu, ndipo mwanenera mtumiki wanu chokoma ichi;

27 chakukomerani kudalitsa nyumba ya mtumiki wanu, kuti ikhalebe kosatha pamaso panu; pakuti Inu Yehova mwadalitsa, ndipo idzadalitsika kosatha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/17-fae521b53822c5add75f6c978a37adba.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 18

Davide akantha Afilisti, Amowabu, Aaramu, ndi Aedomu

1 Ndipo zitatha izi, Davide anakantha Afilisti, nawagonjetsa, nalanda Gati ndi midzi yake m’manja a Afilisti.

2 Anakanthanso Mowabu; ndi Amowabu anakhala anthu a Davide, nabwera nazo mphatso.

3 Ndipo Davide anakantha Hadadezere mfumu ya Zoba ku Hamati, pomuka iye kukhazikitsa ulamuliro wake ku mtsinje wa Yufurate.

4 Ndipo Davide analanda magaleta ake chikwi chimodzi, ndi apakavalo zikwi zisanu ndi ziwiri, ndi oyenda pansi zikwi makumi awiri; Davide anadula mitsita akavalo onse okoka magaleta, koma anasungako ofikira magaleta zana limodzi.

5 Ndipo Aaramu a ku Damasiko anadza kudzathandiza Hadadezere mfumu ya Zoba; koma Davide anakantha Aaramu amuna zikwi makumi awiri mphambu ziwiri.

6 Ndipo Davide anaika asilikali a boma mu Aramu wa Damasiko; ndi Aaramu anasanduka anthu a Davide, nabwera nazo mphatso. Ndipo Yehova anasunga Davide kulikonse anamukako.

7 Natenga Davide zikopa zagolide zinali pa anyamata a Hadadezere, nabwera nazo kuYerusalemu.

8 Ndi ku Tibati, ndi ku Kuni, mizinda ya Hadadezere, Davide anatenga mkuwa wambiri, ndiwo umene Solomoni anayenga nao thawale lamkuwa, ndi nsanamira, ndi zipangizo zamkuwa.

9 Ndipo pakumva Tou, mfumu ya ku Hamati, kuti Davide adakantha khamu lonse la Hadadezere mfumu ya ku Zoba,

10 anatumiza Hadoramu mwana wake kwa mfumu Davide, kumlonjera ndi kumdalitsa, popeza adayambana ndi Hadadezere, namkantha; pakuti Hadadezere adachita nkhondo ndi Tou; ndipo anali nazo zipangizo za mitundumitundu za golide ndisilivandi mkuwa.

11 Izi zomwe mfumu Davide anazipatulira Yehova, pamodzi ndi siliva ndi golide adazitenga kwaamitunduonse, kwa Edomu, ndi kwa Mowabu, ndi kwa ana a Amoni, ndi kwa Afilisti, ndi kwa Amaleke.

12 Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu mu Chigwa cha Mchere zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu.

13 Ndipo anaika asilikali a boma mu Edomu; ndi Aedomu onse anasanduka anthu a Davide. Ndipo Yehova anasunga Davide kulikonse anamukako.

14 Ndipo Davide anakhala mfumu ya Aisraele onse, naweruza anthu ake onse, nawachitira chilungamo.

15 Ndipo Yowabu mwana wa Zeruya anayang’anira khamu la nkhondo, ndi Yehosafati mwana wa Ahiludi anali wolemba mbiri.

16 Ndi Zadoki mwana wa Ahitubi, ndi Ahimeleki mwana wa Abiyatara, anali ansembe, ndi Savisa anali mlembi,

17 ndi Benaya mwana wa Yehoyada anayang’anira Akereti ndi Apeleti; koma ana a Davide ndiwo oyamba ku dzanja la mfumu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/18-5d3e5054328efa7a4db6c3bf11423969.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 19

Davide abwezera chilango kwa Aamoni pa chipongwe chao

1 Ndipo zitatha izi, Nahasi mfumu ya ana a Amoni anamwalira, ndi mwana wake anakhala mfumu m’malo mwake.

2 Ndipo Davide anati, Ndidzamchitira zokoma mtima Hanuni mwana wa Nahasi, popeza atate wake anandichitira ine zokoma mtima. Momwemo Davide anatuma mithenga imtonthoze mtima pa atate wake. Pofika anyamata ake a Davide ku dziko la ana a Amoni kwa Hanuni kumtonthoza mtima,

3 akalonga a ana a Amoni anati kwa Hanuni, Davide ali kuchitira atate wanu ulemu kodi, popeza anakutumizirani otonthoza? Sakudzerani kodi anyamata ake kufunafuna, ndi kugubuduza, ndi kuzonda dziko?

4 Ndipo Hanuni anatenga anyamata a Davide, nawameta, nadula malaya ao pakati kufikira m’matako, nawaleka achoke.

5 Pamenepo anamuka ena namuuza Davide za amunawa. Natumiza iye kukomana nao, pakuti amunawa anachita manyazi kwambiri. Ndipo mfumu inati, Balindani ku Yeriko mpaka zamera ndevu zanu; zitamera mubwere.

6 Ndipo pamene ana a Amoni anaona kuti anadzinunkhitsa kwa Davide, Hanuni ndi ana a Amoni anatumiza matalente chikwi chimodzi asiliva, kudzilembera magaleta ndi apakavalo ku Mesopotamiya, ndi ku Aramu-Maaka, ndi ku Zoba.

7 Momwemo anadzilembera magaleta zikwi makumi atatu mphambu ziwiri, ndi mfumu ya Maaka ndi anthu ake; nadza iwo, namanga misasa chakuno cha Medeba. Ana a Amoni omwe anasonkhana m’mizinda mwao, nadza kunkhondo.

8 Pamene Davide anamva ichi anatuma Yowabu ndi gulu lonse la anthu amphamvu.

9 Ndipo ana a Amoni anatuluka, nandandalitsa nkhondo ku chipata cha mzinda, ndi mafumu adadzawo anali pa okha kuthengo.

10 Pakuona Yowabu tsono kuti nkhondo inamdzera kumaso ndi kumbuyo, anasankha amuna osankhika onse a Israele, nawanika ayambane ndi Aaramu.

11 Ndipo anthu otsala anawapereka m’dzanja la Abisai mbale wake; ndipo anadzinika ayambane ndi ana a Amoni.

12 Ndipo anati, Akandiposa mphamvu Aaramu, udzandilanditsa ndiwe; koma akakuposa mphamvu ana a Amoni, ndidzakulanditsa ndine.

13 Limbika mtima, tilimbikire anthu athu, ndi mizinda ya Mulungu wathu; ndipo Yehova achite chomkomera.

14 Pamenepo Yowabu ndi anthu anali naye anayandikira pamaso pa Aaramu kulimbana nao, ndipo anawathawa.

15 Ndipo pakuona ana a Amoni kuti adathawa Aaramu, iwo omwe anathawa pamaso pa Abisai mbale wake, nalowa m’mzinda. Pamenepo Yowabu anadza kuYerusalemu.

16 Ndipo pakuona Aaramu kuti Israele anawakantha, anatumiza mithenga, natuluka nao Aaramu akukhala tsidya lija la mtsinjewo; ndi Sofaki kazembe wa khamu la Hadadezere anawatsogolera.

17 Ndipo anamuuza Davide; namemeza iye Aisraele onse, naoloka Yordani, nawadzera, nanika nkhondo ayambane nao. Atandandalitsa nkhondo Davide kuyambana ndi Aaramu, anaponyana naye.

18 Ndipo Aaramu anathawa pamaso pa Israele; ndipo Davide anapha Aaramu apamagaleta zikwi zisanu ndi ziwiri, ndi oyenda pansi zikwi makumi anai; napha Sofaki kazembe wa khamulo.

19 Ndipo pakuona anyamata a Hadadezere kuti Israele anawakantha, anapangana mtendere ndi Davide, namtumikira; ndi Aaramu anakana kuthandizanso ana a Amoni.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/19-420b08bacf0edc86afff38fcea584c5f.mp3?version_id=1068—