Categories
1 MBIRI

1 MBIRI Mau Oyamba

Mau Oyamba

Mabuku awiri otchedwa

Mbiri

akambanso zina ndi zina zimene zidakambidwa kale m’mabuku a

Samuele

ndi a

Mafumu

; koma kakambidwe kake nkosiyaniranapo polongosola mbiri ya ufumu wa Israele, chifukwa olemba mabuku a

Mbiri

ali ndi zolinga ziwiri:

1. Afuna kuwonetsa kuti, ngakhale Israele ndi a Yuda adawonongeka kotheratu, Mulungu salephera kuchita zimene analonjeza, mwakuti akuwongolerabe zinthu kudzera mwa anthu okhala mu Yuda, monga momwe adaziganiziratu pa chiyambi. Pofuna kulimbikitsa chiyembekezo chimenechi, olemba mabukuwa akukumbutsa zazikulu zimene adachita Davide ndi Solomoni, ndiponso ntchito za Yehosafati, Hezekiya ndi Yosiya, zothandiza anthu kukhala okhulupirika kwa Mulungu.

2. Afunanso kulongosola za chiyambi cha chipembedzo mu Kachisi wa Yehova ku Yerusalemu, ndiponso za udindo wa ansembe ndi Alevi pa mwambo wa chipembedzo. M’mabuku awiriwo Davide akuwoneka kuti iye ndi mkulu woyambitsa zonsezi, ngakhale amene anamanga Kachisi wa Yehova anali Solomoni.

Buku loyamba la

Mbiri

lifotokoza makamaka za ufumu wa Davide.

Za mkatimu

Mndandanda wa anthu akale ndiponso wa makolo a Israele

1.1—9.44

Imfa ya Saulo

10.1-14

Ufumu wa Davide

11.1—29.30

a. Mavuto ake ndipo ntchito za zazikulu

11.1—22.1

b. Zokonzekera kumanga Kachisi wa Yehova

22.2—29.30

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 1

Maina a makolo kuyambira Adamu kufikira adzukulu a Nowa

1 Adamu, Seti, Enosi,

2 Kenani, Mahalalele, Yaredi,

3 Enoki, Metusela, Lameki,

4 Nowa, Semu, Hamu, ndi Yafeti.

5 Ana a Yafeti: Gomeri, ndi Magogi, ndi Madai, ndi Yavani, ndi Tubala, ndi Meseki, ndi Tirasi.

6 Ndi ana a Gomeri: Asikenazi, Difati, ndi Togarima.

7 Ndi ana a Yavani: Elisa, ndi Tarisisi, Kitimu, ndi Rodanimu.

8 Ana a Hamu: Kusi, ndi Ejipito, Puti, ndi Kanani.

9 Ndi ana a Kusi: Seba, ndi Havila, ndi Sabita, ndi Raama, ndi Sabiteka. Ndi ana a Raama: Sheba, ndi Dedani.

10 Ndi Kusi anabala Nimirodi; iye anayamba kukhala wamphamvu padziko.

11 Ndi Ejipito anabala Aludi, ndi Aanamimu, ndi Alehabu, ndi Anafituhimu,

12 ndi Apatirusi, ndi Akasiluhimu, (kumene anafuma Afilisti), ndi Akafitori.

13 Ndi Kanani anabala Sidoni mwana wake woyamba, ndi Heti,

14 ndi Ayebusi, ndi Aamori, ndi Agirigasi,

15 ndi Ahivi, ndi Aariki, ndi Asini,

16 ndi Aaravadi, ndi Azemari, ndi Ahamati.

17 Ana a Semu: Elamu, ndi Asiriya, ndi Aripakisadi, ndi Ludi, ndi Aramu, ndi Uzi, ndi Huli, ndi Getere, ndi Meseki.

18 Ndi Aripakisadi anabala Sela; ndi Sela anabala Eberi.

19 Ndi Eberi anabala ana aamuna awiri, dzina la winayo ndiye Pelegi, popeza masiku ake dziko linagawanika; ndi dzina la mbale wake ndiye Yokotani.

20 Ndipo Yokotani anabala Alimodadi, ndi Selefi, ndi Hazara-Maveti, ndi Yera;

21 ndi Hadoramu, ndi Uzali, ndi Dikila;

22 ndi Ebala, ndi Abimaele, ndi Sheba,

23 ndi Ofiri, ndi Havila, ndi Yobabu. Awa onse ndiwo ana a Yokotani.

Makolo kuyambira Semu mpaka adzukulu a Abrahamu

24 Semu, Aripakisadi, Sela;

25 Eberi, Pelegi, Reu,

26 Serugi, Nahori, Tera;

27 Abramu, (ndiye Abrahamu).

28 Ana a Abrahamu: Isaki, ndi Ismaele.

Mbumba ya Ismaele

29 Mibadwo yao ndi awa; woyamba wa Ismaele Nebayoti; ndi Kedara ndi Adibeele, ndi Mibisamu,

30 Misima, ndi Duma, Masa, Hadadi, ndi Tema,

31 Yeturi, Nafisi, ndi Kedema. Awa ndi ana a Ismaele.

32 Ndi ana a Ketura mkazi wamng’ono wa Abrahamu anabala Zimirani, ndi Yokisani, ndi Medani, ndi Midiyani, ndi Isibaki, ndi Suwa. Ndi ana a Yokisani: Sheba, ndi Dedani.

33 Ndi ana a Midiyani: Efa, ndi Efere, ndi Hanoki, ndi Abida, ndi Elida. Awa onse ndiwo ana a Ketura.

Mbumba ya Esau

34 Ndipo Abrahamu anabala Isaki. Ana a Isaki: Esau, ndi Israele.

35 Ana a Esau: Elifazi, Reuwele, ndi Yeusi, ndi Yalamu, ndi Kora.

36 Ana a Elifazi: Temani, ndi Omara, Zefi, ndi Gatamu, Kenazi, ndi Timna, ndi Amaleke.

37 Ana a Reuwele: Nahati, Zera, Sama, ndi Miza.

38 Ndi ana a Seiri: Lotani, ndi Sobala, ndi Zibiyoni, ndi Ana, ndi Disoni, ndi Ezere, ndi Disani.

39 Ndi ana a Lotani: Hori, ndi Homamu; ndipo Timna ndiye mlongo wake wa Lotani.

40 Ana a Sobala: Aliyani, ndi Manahati, ndi Ebala, Sefi, ndi Onamu. Ndi ana a Zibiyoni: Aiya ndi Ana.

41 Mwana wa Ana: Disoni. Ndi ana a Disoni: Hamurani, ndi Esibani, ndi Itirani, ndi Kerani.

42 Ana a Ezere: Bilihani, ndi Zaavani, ndi Yaakani. Ana a Disani: Uzi, ndi Arani.

43 Mafumu tsono akuchita ufumu m’dziko la Edomu, pakalibe mfumu wakuchita ufumu pa ana a Israele, ndiwo Bela mwana wa Beori; ndi dzina la mzinda wake ndilo Dinihaba.

44 Ndipo anafa Bela; ndi Yobabu mwana wa Zera wa ku Bozira anakhala mfumu m’malo mwake.

45 Namwalira Yobabu; ndi Husamu wa ku dziko la Atemani anakhala mfumu m’malo mwake.

46 Namwalira Husamu; ndi Hadadi mwana wa Bedadi, amene anakantha Midiyani ku thengo la Mowabu, anakhala mfumu m’malo mwake; ndi dzina la mzinda wake ndi Aviti.

47 Namwalira Hadadi; ndi Samila wa ku Masireka anakhala mfumu m’malo mwake.

48 Namwalira Samila: ndi Shaulo wa ku Rehoboti ku nyanja anakhala mfumu m’malo mwake.

49 Namwalira Shaulo; ndi Baala-Hanani mwana wa Akibori anakhala mfumu m’malo mwake.

50 Namwalira Baala-Hanani; ndi Hadadi anakhala mfumu m’malo mwake; ndipo dzina la mzinda wake ndi Pai; ndi dzina la mkazi wake ndiye Mehetabele mwana wamkazi wa Matiredi mwana wamkazi wa Mezahabu.

51 Namwalira Hadadi. Ndipo mafumu a Edomu ndiwo mfumu Timna, mfumu Aliva, mfumu Yeteti;

52 mfumu Oholibama, mfumu Ela, mfumu Pinoni;

53 mfumu Kenazi, mfumu Temani, mfumu Mibizara;

54 mfumu Magadiele, mfumu Iramu. Awa ndi mafumu a Edomu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/1-1465adbc8db55b47d4b4b9d5da551939.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 2

Ana a Israele, adzukulu a Yuda

1 Ana a Israele ndi awa: Rubeni, Simeoni, Levi, ndi Yuda, Isakara, ndi Zebuloni,

2 Dani, Yosefe, ndi Benjamini, Nafutali, Gadi, ndi Asere.

3 Ana a Yuda ndiwo Eri, ndi Onani, ndi Sela; Batisuwa Mkanani anambalira atatu amenewa. Koma Eri mwana woyamba wa Yuda anali woipa pamaso pa Yehova, ndi Iye anamupha.

4 Ndi Tamara mpongozi wake anambalira Perezi ndi Zera. Ana aamuna onse a Yuda ndiwo asanu.

5 Ana a Perezi: Hezironi, ndi Hamuli.

6 Ndi ana a Zera: Zimiri, ndi Etani, ndi Hemani, ndi Kalikoli, ndi Dara; onse pamodzi ndi asanu.

7 Ndi ana a Karimi: Akara wovuta Israeleyo, amene analakwira choperekedwa chiperekerecho.

8 Ndi mwana wa Etani: Azariya.

9 Ndi ana a Hezironi anambadwirawo: Yerameele, ndi Ramu, ndi Kalebe.

10 Ndi Ramu anabala Aminadabu; ndi Aminadabu anabala Nasoni kalonga wa ana a Yuda;

11 ndi Nasoni anabala Salimoni, ndi Salimoni anabala Bowazi,

12 ndi Bowazi anabala Obedi, ndi Obedi anabala Yese,

13 ndi Yese anabala mwana wake wamwamuna woyamba Eliyabu, ndi Abinadabu wachiwiri, ndi Simea wachitatu,

14 Netanele wachinai, Radai wachisanu,

15 Ozemu wachisanu ndi chimodzi, Davide wachisanu ndi chiwiri;

16 ndi alongo ao ndiwo Zeruya ndi Abigaile. Ndi ana a Zeruya: Abisai ndi Yowabu, ndi Asahele; atatu.

17 Ndi Abigaile anabala Amasa; ndi atate wa Amasa ndiye Yetere Mwismaele.

18 Ndi Kalebe mwana wa Hezironi anabala ana ndi Azuba mkazi wake, ndi Yerioti; ndipo ana ake ndiwo Yesere, ndi Sobabu, ndi Aridoni.

19 Namwalira Azuba, ndi Kalebe anadzitengera Efurata, amene anambalira Huri.

20 Ndi Huri anabala Uri, ndi Uri anabala Bezalele.

21 Ndipo pambuyo pake Hezironi analowa kwa mwana wamkazi wa Makiri atate wa Giliyadi, amene anamtenga akhale mkazi wake, pokhala wa zaka makumi asanu ndi limodzi mwamunayo; ndipo mkaziyo anambalira Segubu.

22 Ndi Segubu anabala Yairi, amene anali nayo mizinda makumi awiri mphambu itatu m’dziko la Giliyadi.

23 Ndi Gesuri ndi Aramu analanda mizinda ya Yairi, pamodzi ndi Kenati ndi midzi yake; ndiyo mizinda makumi asanu ndi limodzi. Iwo onse ndiwo ana a Makiri atate wa Giliyadi.

24 Ndipo atafa Hezironi mu Kalebe-Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anambalira Asiriya atate wa Tekowa.

25 Ndi ana a Yerameele mwana woyamba wa Hezironi ndiwo: woyamba Ramu, ndi Buna, ndi Oreni, ndi Ozemu, ndi Ahiya.

26 Ndipo Yerameele anali naye mkazi wina dzina lake ndiye Atara, ndiye make wa Onamu.

27 Ndipo ana a Ramu mwana woyamba wa Yerameele ndiwo Maazi, ndi Yamini, ndi Ekeri.

28 Ndi ana a Onamu ndiwo Samai, ndi Yada; ndi ana a Samai: Nadabu, ndi Abisuri.

29 Ndipo dzina la mkazi wa Abisuri ndiye Abihaili; ndipo anambalira Abani, ndi Molidi.

30 Ndi ana a Nadabu: Seledi ndi Apaimu; koma Seledi anamwalira wopanda ana.

31 Ndi mwana wa Apaimu: Isi. Ndi mwana wa Isi: Sesani. Ndi mwana wa Sesani: Alai.

32 Ndi ana a Yada mbale wa Samai: Yetere, ndi Yonatani; namwalira Yetere wopanda ana.

33 Ndi ana a Yonatani: Peleti, ndi Zaza. Ndiwo ana a Yerameele.

34 Ndipo Sesani analibe ana aamuna, koma ana aakazi. Ndi Sesani anali naye mnyamata Mwejipito dzina lake ndiye Yara.

35 Ndipo Sesani anampatsa Yara mnyamata wake mwana wake wamkazi akhale mkazi wake, ndipo anambalira Atai.

36 Ndipo Atai anabala Natani, ndi Natani anabala Zabadi,

37 ndi Zabadi anabala Efilala, ndi Efilala anabala Obedi,

38 ndi Obedi anabala Yehu, ndi Yehu anabala Azariya,

39 ndi Azariya anabala Helezi, ndi Helezi anabala Eleasa,

40 ndi Eleasa anabala Sisimai, ndi Sisimai anabala Salumu,

41 ndi Salumu anabala Yekamiya, ndi Yekamiya anabala Elisama.

42 Ndi ana a Kalebe mbale wa Yerameele ndiwo Mesa mwana wake woyamba, ndiye atate wa Zifi; ndi ana a Maresa atate wa Hebroni.

43 Ndi ana a Hebroni: Kora, ndi Tapuwa, ndi Rekemu, ndi Sema.

44 Ndi Sema anabala Rahama atate wa Yorikeamu, ndi Rekemu anabala Samai.

45 Ndi mwana wa Samai ndiye Maoni; ndipo Maoni ndiye atate wa Betezuri.

46 Ndi Efa mkazi wamng’ono wa Kalebe anabala Harani, ndi Moza, ndi Gazezi; ndi Harani anabala Gazezi.

47 Ndi ana a Yadai: Regemu, ndi Yotamu, ndi Gesani, ndi Peleti, ndi Efa, ndi Saafi.

48 Maaka mkazi wamng’ono wa Kalebe anabala Sebere, ndi Tirihana.

49 Iyeyu anabalanso Saafi atate wa Madimana, Seva atate wa Makibena, ndi atate wa Gibea; ndi mwana wamkazi wa Kalebe ndiye Akisa.

50 Ana a Kalebe ndi awa: mwana wa Huri, mwana woyamba wa Efurata, Sobala atate wa Kiriyati-Yearimu.

51 Salima atate wa Betelehemu, Harefi atate wa Betegadere.

52 Ndipo Sobala atate wa Kiriyati-Yearimu anali ndi ana: Harowe, ndi Hazi Amenuwoti.

53 Ndi mabanja a Kiriyati-Yearimu: Aitiri, ndi Aputi, ndi Asumati, ndi Amisrai; Azorati ndi Aestaoli anafuma kwa iwowa.

54 Ana a Salima: Betelehemu, ndi Anetofa, Ataroti-Beti-Yowabu, ndi Hazi Amanahati, ndi Azori.

55 Ndi mabanja a alembi okhala ku Yabezi: Atirati, Asimeati, Asukati. Iwo ndiwo Akeni ofuma ku Hamati, kholo la nyumba ya Rekabu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/2-4575f0a87fd62aa2f3336f627c6ba32e.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 3

Adzukulu a Davide

1 Ana a Davide tsono ombadwira ku Hebroni: woyamba Aminoni wa Ahinowamu wa ku Yezireele, wachiwiri Daniele wa Abigaile wa ku Karimele,

2 wachitatu Abisalomu mwana wa Maaka mwana wamkazi wa Talimai mfumu ya Gesuri, wachinai Adoniya mwana wa Hagiti,

3 wachisanu Sefatiya wa Abitala, wachisanu ndi chimodzi Itireamu wa mkazi wake Egila.

4 Anambadwira asanu ndi mmodzi mu Hebroni; ndi pomwepo anakhala mfumu zaka zisanu ndi ziwiri, ndi miyezi isanu ndi iwiri; ndi muYerusalemuanakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu zitatu.

5 Ndipo ombadwira mu Yerusalemu ndi awa: Simea, ndi Sobabu, ndi Natani, ndi Solomoni, anai a Batisuwa mwana wamkazi wa Amiyele;

6 ndi Ibara, ndi Elisama, ndi Elifeleti,

7 ndi Noga, ndi Nefegi, ndi Yafiya,

8 ndi Elisama, ndi Eliyada, ndi Elifeleti, asanu ndi anai.

9 Onsewa ndiwo ana a Davide, pamodzi ndi ana a akazi aang’ono; ndipo Tamara ndiye mlongo wao.

10 Ndipo mwana wa Solomoni ndiye Rehobowamu, Abiya mwana wake, Asa mwana wake, Yehosafati mwana wake,

11 Yoramu mwana wake, Ahaziya mwana wake, Yowasi mwana wake,

12 Amaziya mwana wake, Azariya mwana wake, Yotamu mwana wake,

13 Ahazi mwana wake, Hezekiya mwana wake, Manase mwana wake,

14 Amoni mwana wake, Yosiya mwana wake.

15 Ndi ana a Yosiya: woyamba Yohanani, wachiwiri Yehoyakimu, wachitatu Zedekiya, wachinai Salumu.

16 Ndi ana a Yehoyakimu: Yekoniya mwana wake, Zedekiya mwana wake.

17 Ndi mwana wa Yekoniya: Asiri, Sealatiele mwana wake,

18 ndi Malikiramu, ndi Pedaya, ndi Senazara, Yekamiya, Hosama, Nedabiya.

19 Ndi ana a Pedaya: Zerubabele ndi Simei; ndi ana a Zerubabele: Mesulamu, ndi Hananiya; ndipo Selomiti ndiye mlongo wao,

20 ndi Hasuba, ndi Ohele, ndi Berekiya, ndi Hasadiya, ndi Yusabu-hesede; asanu.

21 Ndi ana a Hananiya: Pelatiya, ndi Yesaya, ana a Refaya, ana a Arinani, ana a Obadiya, ana a Sekaniya.

22 Ndi mwana wa Sekaniya: Semaya; ndi ana a Semaya: Hatusi, ndi Igala, ndi Bariya, ndi Neariya, ndi Safati; asanu ndi mmodzi.

23 Ndi ana a Neariya: Eliyoenai, ndi Hizikiya, ndi Azirikamu, atatu.

24 Ndi ana a Eliyoenai: Hodaviya, ndi Eliyasibu, ndi Pelaya, ndi Akubu, ndi Yohanani, ndi Delaya, ndi Anani, asanu ndi awiri.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/3-e0b322d726dde0d04c198480c0f34a2f.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 4

Adzukulu a Yuda

1 Ana a Yuda: Perezi, Hezironi, ndi Karimi, ndi Huri, ndi Sobala.

2 Ndipo Reaya mwana wa Sobala anabala Yahati; ndi Yahati anabala Ahumai, ndi Lahadi. Iwo ndiwo mabanja a Azorati.

3 Iwo ndiwo a atate wa Etamu: Yezireele, ndi Isima, ndi Idibasi; ndipo dzina la mlongo wao ndiye Hazeleleponi,

4 ndi Penuwele atate wa Gedori, ndi Ezere atate wa Husa. Awa ndi ana a Huri woyamba wa Efurata atate wa Betelehemu.

5 Ndipo Asiriya atate wa Tekowa anali nao akazi awiri: Hela, ndi Naara.

6 Ndi Naara anambalira Ahuzamu, ndi Hefere, ndi Temeni, ndi Haahasitari. Iwo ndiwo ana a Naara.

7 Ndi ana a Hela ndiwo Zereti, Izihara, ndi Etinani.

8 Ndipo Hakozi anabala Anubu, ndi Zobeba, ndi mabanja a Ahariyele mwana wa Harumu.

9 Ndipo Yabezi analemekezedwa koposa abale ake; ndi make anamutcha dzina lake Yabezi, ndi kuti, Popeza ndambala mwaululu.

10 Ndipo Yabezi anaitana kwa Mulungu wa Israele, ndi kuti, Mundidalitse ndithu, ndi kukulitsa malire anga; ndi dzanja lanu likhale ndi ine, nimundisunge, kuti choipa chisandivute. Ndipo Mulungu anafikitsa chopempha iye.

11 Ndipo Kelubu mbale wa Suha anabala Mehiri, ndiye atate wa Esitoni.

12 Ndi Esitoni, anabala Beterafa, ndi Paseya, ndi Tehina atate wa Irinahasi. Awa ndi anthu a Reka.

13 Ndi ana a Kenazi: Otiniyele, ndi Seraya; ndi mwana wa Otiniyele: Hatati.

14 Ndipo Meonotai anabala Ofura; ndi Seraya anabala Yowabu atate wa Geharasimu; popeza iwo ndiwo amisiri.

15 Ndi ana a Kalebe mwana wa Yefune: Iru, Ela, ndi Naamu; ndi ana a Ela, ndi Kenazi.

16 Ndi ana a Yehalelele: Zifi, ndi Zifa, Tiriya, ndi Asarele.

17 Ndi ana a Ezara: Yetere, ndi Meredi, ndi Efere, ndi Yaloni; ndipo anabala Miriyamu, ndi Samai, ndi Isiba atate wa Esitemowa.

18 Ndi mkazi wake Myuda anabala Yeredi atate wa Gedori, ndi Hebere atate wa Soko, ndi Yekutiyele atate wa Zanowa. Ndipo awa ndi ana a Bitiya mwana wamkazi waFarao, amene Meredi anamtenga.

19 Ndi ana a mkazi wa Hodiya, mlongo wake wa Nahamu, ndiwo atate a Keila Mgarimi ndi Esitemowa Mmaaka.

20 Ndi ana a Simoni; Aminoni, ndi Rina, Benihanani, ndi Tiloni. Ndi ana a Isi: Zoheti, ndi Benizoheti.

21 Ana a Sela mwana wa Yuda: Eri atate wa Leka, ndi Laada atate wa Maresa, ndi mabanja a nyumba ya iwo oomba bafuta wa thonje losansitsa a nyumba ya Asibeya,

22 ndi Yokimu, ndi amuna a Kozeba, ndi Yowasi, ndi Sarafi wolamulira mu Mowabu, ndi Yasubilehemu; koma mau awa ndiwo a kale lomwe.

23 Iwo ndiwo oumba mbiya, ndi okhala mu Netaimu, ndi mu Gedera; anakhala komweko ndi mfumu m’ntchito yake.

Adzukulu a Simeoni

24 Ana a Simeoni: Nemuwele, ndi Yamini, Yaribu, Zera, Shaulo,

25 Salumu mwana wake, Mibisamu mwana wake, Misima mwana wake.

26 Ndi ana a Misima: Hamuele mwana wake, Zakuri mwana wake, Simei mwana wake.

27 Ndipo Simei anali nao ana aamuna khumi mphambu asanu ndi mmodzi, ndi ana aakazi asanu ndi mmodzi; koma abale ake analibe ana ambiri, ndi banja lao lonse silinachulukitse ngati ana a Yuda.

28 Ndipo anakhala ku Beereseba, ndi Molada, ndi Hazara-Suwala,

29 ndi ku Biliha, ndi ku Ezemu, ndi ku Toladi,

30 ndi ku Betuele, ndi ku Horoma, ndi ku Zikilagi,

31 ndi ku Betemara-Kaboti, ndi ku Hazara-Susimu, ndi ku Betebiri, ndi ku Saaraimu. Iyi ndi mizinda yao, mpaka ufumu wa Davide, pamodzi ndi midzi yao.

32 Etamu, ndi Aini, Rimoni, ndi Tokeni, ndi Asani, mizinda isanu;

33 ndi midzi yao yonse pozungulira pake pa mizinda yomweyi, mpakaBaala. Apo ndi pokhala pao ndipo ali nao mawerengedwe a maina ao.

34 Ndi Mesobabu, ndi Yamuleki, ndi Yosa mwana wa Amaziya,

35 ndi Yowele, ndi Yehu mwana wa Yosibiya, mwana wa Seraya, mwana wa Asiyele;

36 ndi Eliyoenai, ndi Yaakoba, ndi Yesohaya, ndi Asaya, ndi Adiyele, ndi Yesimiele, ndi Benaya,

37 ndi Ziza mwana wa Sifi, mwana wa Aloni, mwana wa Yedaya, mwana wa Simiri, mwana wa Semaya;

38 awa otchedwa maina ndiwo akalonga m’mabanja ao, ndi nyumba za makolo ao zinachuluka kwambiri.

39 Ndipo anamuka mpaka polowera ku Gedori kum’mawa kwa chigwa, kufunafuna podyetsa zoweta zao.

40 Ndipo anapeza podyetsa ponenepetsa ndi pabwino, ndipo dzikoli ndi lachitando ndi lodikha ndi losungikamo, pakuti okhalako kale ndiwo a Hamu.

41 Iwo tsono olembedwa maina anadza masiku a Hezekiya mfumu ya Yuda, nakantha mahema ao ndi zokhalamo zao, naziononga konse mpaka lero, nakhala m’malo mwao; popeza panali podyetsa zoweta zao pamenepo.

42 Ndipo ena a iwowa a ana a Simeoni, amuna mazana asanu, ananka kuphiri la Seiri; akuwatsogolera ndiwo Pelatiya, ndi Neariya, ndi Refaya, ndi Uziyele; ana a Isi.

43 Nakantha otsala a Aamaleke adapulumukawo, nakhala komweko mpaka lero lino.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/4-1db62766d48a8477f7ba150e90f9ea95.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 5

Adzukulu a Rubeni

1 Ndipo ana a Rubeni mwana woyamba wa Israele, (pakuti ndiye mwana woyamba; koma popeza anaipsa kama wa atate wake ukulu wake unapatsidwa kwa ana a Yosefe mwana wa Israele, koma m’buku la chibadwidwe asayesedwe monga mwa ukulu wake.

2 Pakuti Yuda anakula mphamvu mwa abale ake, ndi mtsogoleri anafuma kwa iyeyu, koma ukulu ngwa Yosefe);

3 ana a Rubeni mwana woyamba wa Israele: Hanoki, ndi Palu, Hezironi, ndi Karimi.

4 Ana a Yowele: Semaya mwana wake, Gogi mwana wake, Simei mwana wake,

5 Mika mwana wake, Reaya mwana wake, Baala mwana wake,

6 Beera mwana wake, amene Tigilati-Pilesere mfumu ya ku Asiriya anamtenga ndende; ndiye kalonga wa Arubeni.

7 Ndi abale ake monga mwa mabanja ao, powerenga chibadwidwe cha mibadwo yao: akulu ndiwo Yeiyele, ndi Zekariya,

8 ndi Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yowele, wokhala ku Aroere, ndi kufikira ku Nebo ndi Baala-Meoni;

9 ndi kum’mawa anakhala mpaka polowera kuchipululu kuyambira mtsinje wa Yufurate; pakuti zoweta zao zinachuluka m’dziko la Giliyadi.

10 Ndipo masiku a Saulo anagwirana nkhondo ndi Ahagiri, amene adagwa ndi dzanja lao; ndipo anakhala m’mahema mwao kum’mawa konse kwa Giliyadi.

Adzukulu a Gadi

11 Ndi ana a Gadi anakhala pandunji pao m’dziko la Basani mpaka Saleka:

12 Yowele mkulu wao, ndi Safamu wachiwiri, ndi Yanai, ndi Safati mu Basani;

13 ndi abale ao a nyumba za makolo ao: Mikaele, ndi Mesulamu, ndi Sheba, ndi Yorai, ndi Yakani, ndi Ziya, ndi Eberi; asanu ndi awiri.

14 Awa ndi ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Giliyadi, mwana wa Mikaele, mwana wa Yesisai, mwana wa Yado, mwana wa Buzi,

15 Ahi mwana wa Abidiyele, mwana wa Guni, ndiye mkulu wa nyumba za makolo ao.

16 Ndipo anakhala mu Giliyadi mu Basani, ndi m’midzi yake, ndi podyetsa pake ponse pa Saroni, mpaka malire ao.

17 Onsewo anawerengedwa monga mwa mabuku a chibadwidwe chao, masiku a Yotamu mfumu ya Yuda, ndi m’masiku a Yerobowamu mfumu ya Israele.

18 Ana a Rubeni, ndi a Gadi, ndi hafu la fuko la Manase, ngwazi, amuna akugwira chikopa ndi lupanga, ndi kuponya mivi, ozolowera nkhondo, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zinai mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu ndi limodzi akutuluka kunkhondo.

19 Ndipo anagwirana nkhondo ndi Ahagiri, ndi Yeturi, ndi Nafisi, ndi Nodabu.

20 Ndipo anathandizidwa polimbana nao; ndi Ahagiri anaperekedwa m’dzanja lao, ndi onse anali nao; pakuti anafuulira kwa Mulungu pomenyana nao, ndipo anapembedzeka nao, popeza anamkhulupirira Iye.

21 Ndipo analanda zoweta zao,ngamirazao zikwi makumi asanu, ndi nkhosa zikwi mazana awiri ndi makumi asanu, ndi abulu zikwi ziwiri, ndi amuna zikwi zana limodzi.

22 Pakuti adagwa, nafa ambiri, popeza nkhondoyi nja Mulungu. Ndipo anakhala m’malo mwao mpaka anatengedwa ndende.

Adzukulu a Manase kum’mawa

23 Ndi anthu a hafu la fuko la Manase anakhala m’dziko; anachuluka kuyambira Basani kufikira Baala-Heremoni, ndi Seniri, ndi phiri la Heremoni.

24 Ndipo akulu a nyumba za makolo ao ndi awa: Efere, ndi Isi, ndi Eliyele, ndi Aziriele, ndi Yeremiya, ndi Hodaviya, ndi Yadiyele, anthu amphamvu ndithu, anthu omveka, akulu a nyumba za makolo ao.

25 Koma analakwira Mulungu wa makolo ao, nachita chigololo, ndi kutsata milungu ya mitundu ya anthu a m’dziko, amene Mulungu adaononga pamaso pao.

26 Ndipo Mulungu wa Israele anautsa mzimu wa Pulo mfumu ya Asiriya, ndi mzimu wa Tigilati-Pilesere mfumu ya Asiriya, ndiye anawatenga ndende; ndiwo Arubeni, ndi Agadi, ndi hafu la fuko la Manase, nafika nao ku Hala, ndi Habori, ndi Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, mpaka lero lino.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/5-ea3c40941bf41217819a6cd5e9aa101f.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 6

Adzukulu a Levi

1 Ana a Levi: Geresomo, Kohati, ndi Merari.

2 Ndi ana a Kohati: Amuramu, Izihara, ndi Hebroni, ndi Uziyele.

3 Ndi ana a Amuramu: Aroni, ndi Mose, ndi Miriyamu. Ndi ana a Aroni: Nadabu, ndi Abihu, Eleazara, ndi Itamara.

4 Eleazara anabala Finehasi, Finehasi anabala Abisuwa,

5 ndi Abisuwa anabala Buki, ndi Buki anabala Uzi,

6 ndi Uzi anabala Zerahiya, ndi Zerahiya anabala Meraiyoti,

7 Meraiyoti anabala Amariya, ndi Amariya anabala Ahitubi,

8 ndi Ahitubi anabala Zadoki, ndi Zadoki anabala Ahimaazi,

9 ndi Ahimaazi anabala Azariya, ndi Azariya anabala Yohanani,

10 ndi Yohanani anabala Azariya (ndiye amene anachita ntchito ya nsembe m’nyumba anaimanga Solomoni muYerusalemu),

11 ndi Azariya anabala Amariya, ndi Amariya anabala Ahitubi,

12 ndi Ahitubi anabala Zadoki, ndi Zadoki anabala Salumu,

13 ndi Salumu anabala Hilikiya, ndi Hilikiya anabala Azariya,

14 ndi Azariya anabala Seraya, ndi Seraya anabala Yehozadaki,

15 ndi Yehozadaki analowa undende muja Yehova anatenga ndende Yuda ndi Yerusalemu ndi dzanja la Nebukadinezara.

16 Ana a Levi: Geresomo, Kohati ndi Merari.

17 Ndipo maina a ana a Geresomo ndi awa: Libini, ndi Simei.

18 Ndipo ana a Kohati ndiwo Amuramu, ndi Izihara, ndi Hebroni, ndi Uziyele.

19 Ana a Merari: Mali ndi Musi. Ndi mabanja a Alevi monga mwa nyumba za makolo ao ndi awa.

20 Wa Geresomo: Libini mwana wake, Yahati mwana wake, Zima mwana wake,

21 Yowa mwana wake, Ido mwana wake, Zera mwana wake, Yeterai mwana wake.

22 Ana a Kohati: Aminadabu mwana wake, Kora mwana wake, Asiri mwana wake,

23 Elikana mwana wake, ndi Ebiyasafu mwana wake, ndi Asiri mwana wake,

24 Tahati mwana wake, Uriyele mwana wake, Uziya mwana wake, ndi Shaulo mwana wake.

25 Ndi ana a Elikana: Amasai, ndi Ahimoti.

26 Elikana: ana a Elikana Zofai mwana wake, ndi Nahati mwana wake,

27 Eliyabu mwana wake, Yerohamu mwana wake, Elikana mwana wake.

28 Ndi ana a Samuele: woyamba Yowele, ndi wachiwiri Abiya.

29 Ana a Merari: Mali, Libini mwana wake, Simei mwana wake, Uza mwana wake,

30 Simea mwana wake, Hagiya mwana wake, Asaya mwana wake.

A udindo wa kuimba

31 Ndipo iwo aja Davide anawaimika a udindo wa nyimbo m’nyumba ya Yehova, litafikira kupumula likasalo, ndi awa.

32 Ndipo anatumikira ndi kuimba pakhomo pa Kachisi wachihema chokomanakompaka Solomoni adamanga nyumba ya Yehova mu Yerusalemu, naimirira mu utumiki wao monga mwa malongosoledwe ao.

33 Ndipo oimirirawo, ndi ana ao, ndi awa: a ana a Akohati, Hemani woimbayo, mwana wa Yowele, mwana wa Samuele,

34 mwana wa Elikana, mwana wa Yerohamu, mwana wa Eliyele, mwana wa Towa,

35 mwana wa Zufu, mwana wa Elikana, mwana wa Mahati, mwana wa Amasai,

36 mwana wa Elikana, mwana wa Yowele, mwana wa Azariya, mwana wa Zefaniya,

37 mwana wa Tahati, mwana wa Asiri, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora,

38 mwana wa Izihara, mwana wa Kohati, mwana wa Levi, mwana wa Israele.

39 Ndi mbale wake Asafu wokhala ku dzanja lake lamanja, ndiye Asafu mwana wa Berekiya, mwana wa Simea,

40 mwana wa Mikaele, mwana wa Baaseiya, mwana wa Malikiya,

41 mwana wa Etini, mwana wa Zera, mwana wa Adaya,

42 mwana wa Etani, mwana wa Zima, mwana wa Simei,

43 mwana wa Yahati, mwana wa Geresomo, mwana wa Levi.

44 Ndi ku dzanja lamanzere abale ao ana a Merari: Etani mwana wa Kisi, mwana wa Abidi, mwana wa Maluki,

45 mwana wa Hasabiya, mwana wa Amaziya, mwana wa Hilikiya,

46 mwana wa Amizi, mwana wa Bani, mwana wa Semeri,

47 mwana wa Mali, mwana wa Musi, mwana wa Merari, mwana wa Levi.

48 Ndi abale ao Alevi anaikidwa achite za utumiki zilizonse za chihema cha nyumba ya Mulungu.

Ansembe mwa Alevi

49 Koma Aroni ndi ana ake ankafukiza paguwa la nsembe yopsereza, ndi paguwa la nsembe yofukiza, chifukwa cha ntchito yonse ya malo opatulika kwambiri, ndi kuchitira Israele chowatetezera, monga mwa zonse Mose mtumiki wa Mulungu adawauza.

50 Ndipo ana a Aroni ndiwo Eleazara mwana wake, Finehasi mwana wake, Abisuwa mwana wake,

51 Buki mwana wake, Uzi mwana wake, Zerahiya mwana wake,

52 Meraiyoti mwana wake, Amariya mwana wake, Ahitubi mwana wake,

53 Zadoki mwana wake, Ahimaazi mwana wake.

Midzi ya Alevi

54 Pokhala pao tsono monga mwa madera ao m’malire mwao ndi awa: kwa ana a Aroni a mabanja a Akohati, pakuti maere oyamba adagwera iwowa,

55 kwa iwo anapereka Hebroni m’dziko la Yuda, ndi podyetsa pake pozungulira pake;

56 koma minda ya mzinda ndi midzi yake anapatsa Kalebe mwana wa Yefune.

57 Ndi kwa ana a Aroni anapereka mizinda yopulumukirako: Hebroni, ndi Libina ndi mabusa ake, ndi Yatiri, ndi Esitemowa ndi mabusa ake.

58 Ndi Hileni ndi mabusa ake, ndi Debiri ndi mabusa ake,

59 ndi Asani ndi mabusa ake, ndi Betesemesi ndi mabusa ake;

60 ndi ku fuko la Benjamini Geba ndi mabusa ake, ndi Alemeti ndi mabusa ake, ndi Anatoti ndi mabusa ake. Mizinda yao yonse mwa mabanja ao ndiyo mizinda khumi ndi itatu.

61 Ndipo otsala a ana a Kohati analandira mwa maere, motapa pa mabanja a fuko, pa hafu la fuko la Manase, mizinda khumi.

62 Ndi kwa ana a Geresomo monga mwa mabanja ao, motapa pa fuko la Isakara, ndi pa fuko la Asere, ndi pa fuko la Nafutali, ndi pa fuko la Manase mu Basani, mizinda khumi ndi itatu.

63 Ana a Merari analandira mwa maere monga mwa mabanja ao, motapa pa fuko la Rubeni, ndi pa fuko la Gadi, ndi pa fuko la Zebuloni, mizinda khumi ndi iwiri.

64 Ndipo ana a Israele anapatsa Alevi mizinda ndi mabusa ao.

65 Ndipo anapatsa mwamaere, motapa pa fuko la ana a Yuda, ndi pa fuko la Simeoni, ndi pa fuko la ana a Benjamini, mizinda iyi yotchulidwa maina ao.

66 Ndi mabanja ena a ana a Kohati anali nayo mizinda ya malire ao, yotapa pa fuko la Efuremu.

67 Ndipo anawapatsa mizinda yopulumukiramo: Sekemu ndi mabusa ake ku mapiri a Efuremu, Gezere ndi mabusa ake,

68 ndi Yokomeamu ndi mabusa ake, ndi Betehoroni ndi mabusa ake,

69 ndi Ayaloni ndi mabusa ake, ndi Gatirimoni ndi mabusa ake,

70 ndi motapa pa hafu la fuko la Manase, Anere ndi mabusa ake, ndi Bileamu ndi mabusa ake, kwa otsala a mabanja a ana a Kohati.

71 Ana a Geresomo analandira motapa pa mabanja a hafu la fuko la Manase, Golani mu Basani ndi mabusa ake, ndiAsitarotindi mabusa ake;

72 ndi motapa pa fuko la Isakara, Kedesi ndi mabusa ake, Daberati ndi mabusa ake,

73 ndi Ramoti ndi mabusa ake, ndi Anemu ndi mabusa ake;

74 ndi motapa pa fuko la Asere, Masala ndi mabusa ake, ndi Abidoni ndi mabusa ake,

75 ndi Hukoki ndi mabusa ake, ndi Rehobu ndi mabusa ake;

76 ndi motapa pa fuko la Nafutali, Kedesi mu Galileya ndi mabusa ake, ndi Hamoni ndi mabusa ake, ndi Kiriyataimu ndi mabusa ake.

77 Amerari (otsala a Alevi) analandira, motapa pa fuko la Zebuloni, Rimoni ndi mabusa ake, Tabori ndi mabusa ake;

78 ndi tsidya lija la Yordani kum’mawa kwa Yeriko analandira, motapa pa fuko la Rubeni, Bezeri m’chipululu ndi mabusa ake, ndi Yahazi ndi mabusa ake,

79 ndi Kedemoti ndi mabusa ake, ndi Mefaati ndi mabusa ake;

80 ndi motapa m’fuko la Gadi, Ramoti mu Giliyadi ndi mabusa ake, ndi Mahanaimu ndi mabusa ake,

81 ndi Hesiboni ndi mabusa ake, ndi Yazere ndi mabusa ake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/6-f91a373f1650ccac8d012d80219418c8.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 7

Adzukulu a Isakara

1 Ana a Isakara ndiwo Tola, ndi Puwa, Yasubu ndi Simironi; anai.

2 Ndi ana a Tola: Uzi, ndi Refaya, ndi Yeriyele, ndi Yamai, ndi Ibisamu, ndi Semuele, akulu a nyumba za makolo; ao ndiwo a Tola, ngwazi zamphamvu, m’mibadwo yao; kuwerenga kwao, masiku a Davide ndiko zikwi makumi awiri mphambu ziwiri kudza mazana asanu ndi limodzi.

3 Ndi mwana wa Uzi: Izrahiya; ndi ana a Izrahiya: Mikaele, ndi Obadiya, ndi Yowele, ndi Isiya; onse asanuwa ndiwo akulu.

4 Ndi pamodzi nao mwa mibadwo yao, mwa nyumba za makolo ao, panali magulu a nkhondo zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi chimodzi, popeza anachuluka akazi ao ndi ana ao.

5 Ndi abale ao mwa mabanja onse a Isakara, ngwazi zamphamvu, oyesedwa mwa chibadwidwe chao, onsewa ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu mphambu zisanu ndi ziwiri.

Adzukulu a Benjamini ndi Nafutali

6 Ana a Benjamini ndiwo Bela, ndi Bekere, ndi Yediyaele, atatu.

7 Ndi ana a Bela: Eziboni, ndi Uzi, ndi Uziyele, ndi Yerimoti, ndi Iri, asanu; akulu a nyumba za makolo ao, ngwazi zamphamvu, owerengedwa m’mabuku a chibadwidwe zikwi makumi awiri mphambu ziwiri kudza makumi atatu ndi anai.

8 Ndi ana a Bekere: Zimira, ndi Yowasi, ndi Eliyezere, ndi Eliyoenai, ndi Omuri, ndi Yeremoti, ndi Abiya, ndi Anatoti, ndi Alemeti. Onsewa ndiwo ana a Bekere.

9 Ndipo anayesedwa mwa chibadwidwe chao, mwa mibadwo yao, akulu a nyumba za makolo ao, ngwazi zamphamvu zikwi makumi awiri mphambu mazana awiri.

10 Ndi mwana wa Yediyaele: Bilihani; ndi ana a Bilihani: Yeusi, ndi Benjamini, ndi Ehudi, ndi Kenana, ndi Zetani, ndi Tarisisi, ndi Ahisahara.

11 Onsewa ndiwo ana a Yediyaele; ndiwo akulu a nyumba za makolo ao, ngwazi zamphamvu zikwi khumi mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana awiri akutuluka kugulu kunkhondo.

12 Supimu yemwe ndi Hupimu ana a Iri, ndi Husimu mwana wa Aheri.

13 Ana a Nafutali: Yaziyele, ndi Guni, ndi Yezere, ndi Salumu, ana a Biliha.

Adzukulu a Manase

14 Ana a Manase ndiwo Asiriele amene mkazi wake anambala. Koma mkazi wake wamng’ono Mwaramu anabala Makiri atate wa Giliyadi;

15 ndi Makiri anadzitengera mkazi, mlongo wake wa Hupimu ndi Supimu, dzina lake ndiye Maaka. Ndipo dzina la mwana wachiwiri wa Manase ndiye Zelofehadi. Ndi Zelofehadi anali ndi ana aakazi.

16 Ndi Maaka mkazi wa Makiri anabala mwana, namutcha dzina lake Peresi, ndi dzina la mbale wake ndiye Seresi, ndi ana ake ndiwo Ulamu, ndi Rakemu.

17 Ndi mwana wa Ulamu: Bedani; ndiwo ana a Giliyadi mwana wa Makiri mwana wa Manase.

18 Ndi mlongo wake Hamoleketi anabala Isihodi, ndi Abiyezere, ndi Mala.

19 Ndi ana a Semida ndiwo Ahiyani, ndi Sekemu, ndi Liki, ndi Aniyamu.

A Efuremu

20 Ndi ana a Efuremu: Sutela, ndi Beredi mwana wake, ndi Tahati mwana wake, ndi Eleada mwana wake, ndi Tahati mwana wake,

21 ndi Zabadi mwana wake, ndi Sutela mwana wake, ndi Ezere, ndi Eleadi, amene anthu a Gati obadwa m’dziko anamupha, popeza anatsikira kukalanda zoweta zao.

22 Ndipo Efuremu atate wao, anachita maliro masiku ambiri, ndi abale ake anadza kudzamtonthoza mtima.

23 Ndipo analowa kwa mkazi wake, naima iye, nabala mwana, namutcha dzina lake Beriya, popeza m’nyumba mwake mudaipa.

24 Ndipo mwana wake wamkazi ndiye Seera, amene anamanga Betehoroni wa kunsi, ndi Betehoroni wa kumtunda, ndi Uzeniseera.

25 Ndipo Refa anali mwana wake, ndi Resefi, ndi Tela mwana wake, ndi Tahani mwana wake,

26 Ladani mwana wake, Amihudi mwana wake, Elisama mwana wake,

27 Nuni mwana wake, Yoswa mwana wake.

28 Ndipo dziko lao, ndi pokhala pao ndizo Betele ndi midzi yake, ndi kum’mawa Naarani, ndi kumadzulo Gezere ndi midzi yake, ndi Sekemu ndi midzi yake, mpaka Aya ndi midzi yake;

29 ndi kumalire a ana a Manase; Beteseani ndi midzi yake, Taanaki ndi midzi yake, Megido ndi midzi yake, Dori ndi midzi yake. M’menemo anakhala ana a Yosefe mwana wa Israele.

30 Ana a Asere: Imina, ndi Isiva, ndi Isivi, ndi Beriya, ndi Sera mlongo wao.

31 Ndi ana a Beriya: Hebere, ndi Malikiele, ndiye atate wa Birizaiti.

32 Ndi Hebere anabala Yafileti, ndi Somere, ndi Hotamu, ndi Suwa mlongo wao.

33 Ndi ana a Yafileti: Pasaki, ndi Bimala, ndi Asivati. Awa ndi ana a Yafileti.

34 Ndi ana a Semeri: Ahi, ndi Roga, Yehuba, ndi Aramu.

35 Ndi ana a Helemu mbale wake: Zofa, ndi Imina, ndi Selesi, ndi Amala.

36 Ana a Zofa: Suwa, ndi Harenefere, ndi Suwala, ndi Beri, ndi Imira,

37 Bezere, ndi Hodi, ndi Sama, ndi Silisa, ndi Itirani, ndi Beera.

38 Ndi ana a Yetere: Yefune, ndi Pisipa, ndi Ara.

39 Ndi ana a Ula: Ara, ndi Haniyele, ndi Riziya.

40 Awa onse ndiwo ana a Asere, akulu a nyumba za makolo ao, ngwazi zosankhika ndi zamphamvu, akulu mwa akalonga. Oyesedwa mwa chibadwidwe chao otumikira kunkhondo ndiwo amuna zikwi makumi awiri mphambu zisanu ndi chimodzi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/7-41a092f5408252ab37e1d270a1c9bba8.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 8

Adzukulu a Benjamini ndi Saulo

1 Ndipo Benjamini anabala Bela mwana wake woyamba, Asibele wachiwiri, ndi Ahara wachitatu,

2 Noha wachinai, ndi Rafa wachisanu.

3 Ndi Bela anali ndi ana: Adara, ndi Gera, ndi Abihudi,

4 ndi Abisuwa, ndi Naamani, ndi Ahowa,

5 ndi Gera, ndi Sefufani, ndi Huramu.

6 Ndi ana a Ehudi ndi awa: ndiwo akulu a nyumba za makolo ao a iwo okhala ku Geba, ndipo anawatenga ndende kunka ku Manahati,

7 natenga ndende Naamani, ndi Ahiya, ndi Gera, ndipo, anabala Uza, ndi Ahihudi.

8 Ndipo Saharaimu anabala ana ku dziko la Mowabu, atachotsa akazi ake Husimu ndi Baara.

9 Ndipo Hodesi mkazi wake anambalira Yobabu, ndi Zibiya, ndi Mesa, ndi Malikamu,

10 ndi Yeuzi, ndi Sakiya, ndi Mirima. Awa ndi ana ake aakulu a nyumba za makolo ao.

11 Ndi Husimu anambalira Abitubu, ndi Elipaala.

12 Ndi ana a Elipaala: Eberi, ndi Misamu, ndi Semedi, amene anamanga Ono, ndi Lodi ndi midzi yake,

13 ndi Beriya, ndi Sema; ndiwo akulu a nyumba za makolo a iwo okhala mu Ayaloni, amene anathawitsa okhala mu Gati;

14 ndi Ahiyo, Sasaki, ndi Yeremoti,

15 ndi Zebadiya, ndi Aradi, ndi Edere,

16 ndi Mikaele, ndi Isipa, ndi Yoha, ana a Beriya;

17 ndi Zebadiya, ndi Mesulamu, ndi Hiziki, ndi Hebere,

18 ndi Isimerai, ndi Iziliya, ndi Yobabu, ana a Elipaala;

19 ndi Yakimu, ndi Zikiri, ndi Zabidi,

20 ndi Eliyenai, ndi Ziletai, ndi Eliyele,

21 ndi Adaya, ndi Beraya, ndi Simiratu, ana a Simei;

22 ndi Isipani, ndi Eberi, ndi Eliyele,

23 ndi Abidoni, ndi Zikiri, ndi Hanani,

24 ndi Hananiya, ndi Elamu, ndi Antotiya,

25 ndi Ifidea, ndi Penuwele, ana a Sasaki;

26 ndi Samuserai, ndi Sehariya, ndi Ataliya,

27 ndi Yaaresiya ndi Eliya, ndi Zikiri, ana a Yerohamu.

28 Awa ndi akulu a nyumba za makolo mwa mibadwo yao, ndiwo akulu anakhala muYerusalemuawa.

29 Ndipo mu Gibiyoni anakhala atate a Gibiyoni, dzina la mkazi wake ndiye Maaka;

30 ndi mwana wake woyamba ndiye Abidoni, opondana naye ndi Zuri, ndi Kisi, ndi Baala, ndi Nadabu,

31 ndi Gedori, ndi Ahiyo, ndi Zekeri.

32 Ndipo Mikiloti anabala Simea. Ndi iwonso anakhala pamodzi ndi abale ao mu Yerusalemu, popenyana ndi abale ao.

33 Ndipo Nere anabala Kisi, ndi Kisi anabala Saulo, ndi Saulo anabala Yonatani, ndi Malikisuwa, ndi Abinadabu, ndi Esibaala.

34 Ndi mwana wa Yonatani, ndiye Meribaala; ndi Meribaala anabala Mika.

35 Ndi ana a Mika: Pitoni, ndi Meleki, ndi Tareya, ndi Ahazi.

36 Ndi Ahazi anabala Yehoyada, ndi Yehoyada anabala Alemeti, ndi Azimaveti, ndi Zimiri; ndi Zimiri anabala Moza;

37 ndi Moza anabala Bineya, mwana wake ndiye Rafa, mwana wake Eleasa, mwana wake Azele;

38 ndipo Azele anali nao ana asanu ndi mmodzi, maina ao ndiwo Azirikamu, Bokeru, ndi Ismaele, ndi Seyariya, ndi Obadiya, ndi Hanani. Onsewa ndiwo ana a Azele.

39 Ndipo ana a Eseki mbale wake: Ulamu mwana wake woyamba, Yeusi wachiwiri, ndi Elifeleti wachitatu.

40 Ndipo ana a Ulamu ndiwo ngwazi zamphamvu, ndiwo oponya mivi, nakhala nao ana ambiri ndi zidzukulu zana limodzi. Onsewa ndiwo a ana a Benjamini.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/8-8eb82e0f6e5539828723bda2608c89df.mp3?version_id=1068—

Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 9

Okhala mu Yerusalemu atabwera kuchokera ku Babiloni

1 Ndipo Aisraele onse anawerengedwa mwa chibadwidwe chao; ndipo taonani, alembedwa m’buku la mafumu a Israele; ndipo Yuda anatengedwa ndende kunka ku Babiloni chifukwa cha kulakwa kwao.

2 Okhala m’dziko oyamba tsono, akukhala mwaomwao m’mizinda mwao, ndiwo Israele, ansembe, Alevi, ndi Antchito a m’kachisi.

3 Ndipo muYerusalemumunakhala a ana a Yuda, ndi a ana a Benjamini, ndi a ana a Efuremu ndi Manase:

4 Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omuri, mwana wa Imuri, mwana wa Bani, wa ana a Perezi mwana wa Yuda.

5 Ndipo a Asiloni: Asaya woyamba, ndi ana ake.

6 Ndi a ana a Zera: Yeuwele ndi abale ao mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi anai.

7 Ndi a ana a Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodaviya, mwana wa Hasenuwa;

8 ndi Ibineya mwana wa Yerohamu, ndi Ela mwana wa Uzi, mwana wa Mikiri, ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reuwele, mwana wa Ibineya,

9 ndi abale ao monga mwa mibadwo yao mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi. Onsewa ndiwo akulu a nyumba za makolo ao m’nyumba za makolo ao.

10 Ndi a ansembe: Yedaya, ndi Yehoyaribu, ndi Yakini,

11 ndi Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Meraiyoti, mwana wa Ahitubi, mtsogoleri wa m’nyumba ya Mulungu;

12 ndi Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasuri, mwana wa Malikiya, ndi Maasai mwana wa Adiyele, mwana wa Yazera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemiti, mwana wa Imeri,

13 ndi abale ao, akulu a nyumba za makolo ao chikwi chimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu ndi limodzi, anthu odziwitsitsa ntchito ya utumiki wa nyumba ya Mulungu.

14 Ndi a Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, a ana a Merari;

15 ndi Bakibakara, Heresi, ndi Galali, ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;

16 ndi Obadiya mwana wa Semaya, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni, ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, wokhala m’midzi ya Anetofa.

17 Ndi odikira pakhomo: Salumu, ndi Akubu, ndi Talimoni, ndi Ahimani ndi abale ao; Salumu ndi mkulu wao,

18 amene adadikira pa chipata cha mfumu kum’mawa mpaka pomwepo, ndiwo odikira pakhomo a tsasa la ana a Levi.

19 Ndipo Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora, ndi abale ake a nyumba ya atate wake; Akora anayang’anira ntchito ya utumiki, osunga zipata za Kachisi monga makolo ao; anakhala m’chigono cha Yehova osunga polowera;

20 ndi Finehasi mwana wa Eleazara anali mtsogoleri wao kale, ndipo Yehova anali naye.

21 Zekariya mwana wa Meselemiya anali wodikira pakhomo pachihema chokomanako.

22 Iwo onse osankhidwa akhale odikira kuzipata ndiwo mazana awiri mphambu khumi ndi awiri. Iwo anawerengedwa monga mwa chibadwidwe chao, m’midzi mwao, amene Davide ndi Samuele mlauli anawaika mu udindo wao.

23 Momwemo iwo ndi ana ao anayang’anira zipata za kunyumba ya Yehova, ndiyo nyumba ya Kachisi, mu udikiro wao.

24 Pa mbali zinai panali odikira kum’mawa, kumadzulo, kumpoto, ndi kumwera.

25 Ndi abale ao m’midzi mwao akafikafika, atapita masiku asanu ndi awiri masabata onse, kuti akhale nao;

26 pakuti odikira anai aakulu, ndiwo Alevi, anali mu udindo wao, nayang’anira zipinda ndi mosungiramo chuma m’nyumba ya Mulungu.

27 Ndipo amagona usiku m’zipinda zozinga nyumba ya Mulungu, popeza udikiro wake ndi wao; kuitsegula m’mawa ndi m’mawa ndi kwaonso.

28 Ndi ena a iwo anayang’anira zipangizo za utumikiwo, pakuti analowa nazo ataziwerenga, natuluka nazo ataziwerenga.

29 Ndi ena a iwo anaikidwa ayang’anire zipangizo zilizonse, ndi zipangizo zonse za malo opatulika, ndi ufa wosalala, ndi vinyo, ndi mafuta, ndilubani, ndi zonunkhira.

30 Ndi ana ena a ansembe anasakaniza chisakanizo cha zonunkhira.

31 Ndi Matitiya wina wa Alevi, ndiye mwana woyamba wa Salumu Mkora, anaikidwa ayang’anire zokazingidwa m’ziwaya.

32 Ndi ena a abale ao, a ana a Akohati, anayang’anira mkate woonekera, kuukonza masabata onse.

33 Ndipo awa ndi oimba, akulu a nyumba za makolo a Alevi, okhala m’zipinda, omasuka ku ntchito zina; pakuti anali nayo ntchito yao usana ndi usiku.

34 Awa ndi akulu a nyumba za makolo a Alevi mwa mibadwo yao, ndiwo akulu; anakhala ku Yerusalemu awa.

35 Ndipo mu Gibiyoni munakhala atate wa Gibiyoni Yeiyele, dzina la mkazi wake ndiye Maaka;

36 ndi mwana wake woyamba ndiye Abidoni, opondana naye ndi Zuri, ndi Kisi, ndi Baala, ndi Nere, ndi Nadabu,

37 ndi Gedori, ndi Ahiyo, ndi Zekariya, ndi Mikiloti.

38 Ndi Mikiloti anabala Simeamu. Ndipo iwonso anakhala pamodzi ndi abale ao mu Yerusalemu, pandunji pa abale ao.

39 Ndipo Nere anabala Kisi, ndi Kisi anabala Saulo, ndi Saulo anabala Yonatani, ndi Malikisuwa, ndi Abinadabu, ndi Esibaala.

40 Ndipo mwana wa Yonatani ndiye Meribaala; ndi Meribaala anabala Mika.

41 Ndi ana a Mika: Pitoni, ndi Meleki, ndi Tareya, ndi Ahazi.

42 Ndi Ahazi anabala Yara, ndi Yara anabala Alemeti, ndi Azimaveti, ndi Zimiri; ndi Zimiri anabala Moza,

43 ndi Moza anabala Bineya, ndi Refaya mwana wake, Eleasa mwana wake, Azele mwana wake;

44 ndi Azele anali nao ana asanu ndi mmodzi, maina ao ndi awa; Azirikamu, Bokeru, ndi Ismaele, ndi Seyariya, ndi Obadiya, ndi Hanani; awa ndi ana a Azele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/9-4303660597a0061ca985207e66f2b5e2.mp3?version_id=1068—