Categories
2 TIMOTEO

2 TIMOTEO 1

1 PaulomtumwiwaKhristuYesu mwa chifuniro cha Mulungu, monga mwa lonjezano la moyo wa mu Khristu Yesu,

2 kwa Timoteo, mwana wanga wokondedwa: Chisomo, chifundo, mtendere za kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye wathu.

Chikondi cha Paulo cha pa Timoteo

3 Ndiyamika Mulungu, amene ndimtumikira kuyambira makolo anga ndi chikumbumtima choyera, kuti ndikumbukira iwe kosalekeza m’mapemphero anga,

4 pokhumba usiku ndi usana kukuona iwe, ndi kukumbukira misozi yako, kuti ndidzazidwe nacho chimwemwe;

5 pokumbukira chikhulupiriro chosanyenga chili mwa iwe, chimene chinayamba kukhala mwa agogo ako Loisi, ndi mwa mai wako Yunisi, ndipo, ndakopeka mtima, mwa iwenso.

6 Chifukwa chake ndikukumbutsa iwe ukoleze mphatso ya Mulungu, ili mwa iwe mwa kuika kwa manja anga.

7 Pakuti Mulungu sanatipatse mzimu wa mantha; komatu wa mphamvu ndi chikondi ndi chidziletso.

8 Potero usachite manyazi pa umboni wa Ambuye wathu, kapena pa ine wandende wake; komatu umve masautso ndi Uthenga Wabwino, monga mwa mphamvu ya Mulungu;

9 amene anatipulumutsa ife, natiitana ife ndi maitanidwe oyera, si monga mwa ntchito zathu, komatu monga mwa chitsimikizo mtima cha Iye yekha, ndi chisomo, chopatsika kwa ife mwa Khristu Yesu nthawi zisanayambe,

10 koma chaonetsedwa tsopano m’maonekedwe a Mpulumutsi wathu Khristu Yesu, amenedi anatha imfa, naonetsera poyera moyo ndi chosavunda mwa Uthenga Wabwino,

11 umene ndaikikapo mlaliki, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wake.

12 Chifukwa cha ichicho ndinamva zowawa izi; komatu sindichita manyazi; pakuti ndimdziwa Iye amene ndamkhulupirira, ndipo ndikopeka mtima kuti ali wa mphamvu ya kudikira chosungitsa changacho kufikira tsiku lijalo.

13 Gwira chitsanzo cha mau a moyo, amene udawamva kwa ine, mwa chikhulupiriro ndi chikondi chili mwa Khristu Yesu.

14 Chosungitsa chokomacho udikire mwa Mzimu Woyera amene akhalitsa mwa ife.

15 Ichi uchidziwa, kuti onse a mu Asiya adabwerera kusiyana nane; a iwo ali Figelo ndi Heremogene.

16 Ambuye achitire banja la Onesifore chifundo; pakuti anatsitsimutsa ine kawirikawiri, ndipo sanachite manyazi ndi unyolo wanga;

17 komatu pokhala mu Roma iye anandifunafuna ine ndi khama, nandipeza.

18 (Ambuye ampatse iye apeze chifundo ndi Ambuye tsiku lijalo); ndi muja ananditumikira m’zinthu zambiri mu Efeso, uzindikira iwe bwino.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2TI/1-3817ba401e4e0c6950a071ca38b51a6c.mp3?version_id=1068—

Categories
2 TIMOTEO

2 TIMOTEO 2

1 Ndipo iwe, mwana wanga, limbika m’chisomo cha mwaKhristuYesu.

2 Ndipo zimene wazimva kwa ine mwa mboni zambiri, zomwezi uikize kwa anthu okhulupirika, amene adzadziwa kuphunzitsa enanso.

3 Umve zowawa pamodzi nane monga msilikali wabwino wa Khristu Yesu.

4 Msilikali sakodwa nazo ntchito wamba, kuti akakondweretse iye amene adamlemba usilikali.

5 Koma ngatinso wina ayesana nao m’makani amasewero, samveka korona ngati sanayesane monga adapangana.

6 Wam’munda wogwiritsitsa ntchitoyo ayenera akhale woyamba kulandira zipatsozo.

7 Lingirira chimene ndinena; pakuti Ambuye adzakupatsa chidziwitso m’zonse.

8 Kumbukira Yesu Khristu, wouka kwa akufa, wochokera m’mbeu ya Davide, monga mwa Uthenga Wabwino wanga;

9 m’menemo ndimva zowawa kufikira zomangira, monga wochita zoipa; koma mau a Mulungu samangika.

10 Mwa ichi ndipirira zonse, chifukwa cha osankhika, kuti iwonso akapeze chipulumutsocho cha mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi ulemerero wosatha.

11 Okhulupirika mauwa: Pakuti ngati tidamwalira ndi Iye, tidzakhalanso moyo ndi Iye:

12 ngati tipirira, tidzachitanso ufumu ndi Iye: ngati timkana Iye, Iyeyunso adzatikana ife:

13 ngati tikhala osakhulupirika, Iyeyu akhala wokhulupirika; pakuti sangathe kudzikana yekha.

Umo azichita ndi osochera

14 Uwakumbutse izi, ndi kuwachitira umboni pamaso pa Ambuye, kuti asachite makani ndi mau osapindulitsa kanthu, koma ogwetsa iwo akumva.

15 Uchite changu kudzionetsera kwa Mulungu wovomerezeka, wantchito wopanda chifukwa cha kuchita manyazi, wolunjika nao bwino mau a choonadi.

16 Koma pewa nkhani zopanda pake; pakuti adzapitirira kutsata chisapembedzo,

17 ndipo mau ao adzanyeka chilonda; a iwo ali Himeneo ndi Fileto;

18 ndiwo amene adasokera kunena za choonadi, ponena kuti kuuka kwa akufa kwachitika kale, napasula chikhulupiriro cha ena.

19 Koma ndithu maziko a Mulungu aimika pokhazikika, ndi kukhala nacho chizindikiro ichi, Ambuye azindikira iwo amene ali ake; ndipo, Adzipatule kwa chosalungama yense wakutchula dzina la Ambuye.

20 Koma m’nyumba yaikulu simuli zotengera za golide ndisilivazokha, komatunso za mtengo ndi dothi; ndipo zina zaulemu, koma zina zopanda ulemu.

21 Ngati tsono munthu adziyeretsa yekha pa izi, adzakhala chotengera cha kuulemu, chopatulidwa, choyenera kuchita nacho Mbuye, chokonzera ntchito yonse yabwino.

22 Koma thawa zilakolako za unyamata, nutsate chilungamo, chikhulupiriro, chikondi, mtendere, pamodzi ndi iwo akuitana pa Ambuye ndi mitima yoyera.

23 Koma mafunso opusa ndi opanda malango upewe, podziwa kuti abala ndeu.

24 Ndipo kapolo wa Ambuye sayenera kuchita ndeu, komatu akhale woyenera, waulere pa onse, wodziwa kuphunzitsa, woleza,

25 wolangiza iwo akutsutsana mofatsa; ngati kapena Mulungu awapatse iwo chitembenuziro, kukazindikira choonadi,

26 ndipo akadzipulumutse kumsampha wa mdierekezi, m’mene anagwidwa naye, kuchifuniro chake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2TI/2-f999249bd350206181f893226ccd5431.mp3?version_id=1068—

Categories
2 TIMOTEO

2 TIMOTEO 3

Zoipa zoopsa masiku otsiriza

1 Koma zindikira ichi, kuti masiku otsiriza zidzafika nthawi zowawitsa.

2 Pakuti anthu adzakhala odzikonda okha, okonda ndalama, odzitamandira, odzikuza, amwano, osamvera akuwabala, osayamika,

3 osayera mtima, opanda chikondi chachibadwidwe, osayanjanitsika, akudierekeza, osakhoza kudziletsa, aukali, osakonda abwino,

4 achiwembu, aliuma olimbirira, otukumuka mtima, okonda zokondweretsa munthu, osati okonda Mulungu;

5 akukhala nao maonekedwe a chipembedzo, koma mphamvu yake adaikana; kwa iwonso udzipatule.

6 Pakuti mwa iwo akhala akukwawira m’nyumba, nagwira akazi opusa, osenza akatundu a zoipa zao, otengedwa nazo zilakolako za mitundumitundu:

7 ophunzira nthawi zonse, koma sangathe konse kufikira kuchizindikiritso cha choonadi.

8 Ndipo monga momwe Yane ndi Yambere anatsutsana naye Mose, kotero iwonso atsutsana nacho choonadi; ndiwo anthu ovunditsitsa mtima, osatsimikizidwa pachikhulupiriro.

9 Koma sadzapitirirapo; pakuti kupusa kwao kudzaonekeratu kwa onse, monganso kupusa kwa iwo aja.

Timoteo alimbike kutsata ziphunzitso zokoma, ndi kulalikira nthawi zonse

10 Koma iwe watsatatsata chiphunzitso changa, mayendedwe, chitsimikizo mtima, chikhulupiriro, kuleza mtima, chikondi, chipiriro,

11 mazunzo, kumva zowawa; zotere zonga anandichitira mu Antiokeya, mu Ikonio, mu Listara, mazunzo otere onga ndawamva; ndipo m’zonsezi Ambuye anandilanditsa.

12 Ndipo onse akufuna kukhala opembedza m’moyo mwaKhristuYesu, adzamva mazunzo.

13 Koma anthu oipa ndi onyenga, adzaipa chiipire, kusokeretsa ndi kusokeretsedwa.

14 Koma ukhalebe iwe mu izi zimene waziphunzira, nutsimikizika mtima nazo, podziwa amene adakuphunzitsa;

15 ndi kuti kuyambira ukhanda wako wadziwa malembo opatulika, okhoza kukupatsa nzeru kufikira chipulumutso, mwa chikhulupiriro cha mwa Khristu Yesu.

16 Lemba lililonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero, chilangizo cha m’chilungamo:

17 kuti munthu wa Mulungu akhale woyenera, wokonzeka kuchita ntchito iliyonse yabwino.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2TI/3-efb88345e68f2a513c14933713db81e2.mp3?version_id=1068—

Categories
2 TIMOTEO

2 TIMOTEO 4

1 Ndikuchitira umboni pamaso pa Mulungu ndiKhristuYesu, amene adzaweruza amoyo ndi akufa, ndi pa maonekedwe ake ndi ufumu wake;

2 lalikira mau; chita nao pa nthawi yake, popanda nthawi yake; tsutsa, dzudzula, chenjeza, ndi kuleza mtima konse ndi chiphunzitso.

3 Pakuti idzafika nthawi imene sadzalola chiphunzitso cholamitsa; komatu poyabwa m’khutu adzadziunjikitsa aphunzitsi monga mwa zilakolako za iwo okha:

4 ndipo adzalubza dala pachoonadi, nadzapatukira kutsata nthano zachabe.

5 Koma iwe, khala maso m’zonse, imva zowawa, chita ntchito ya mlaliki wa Uthenga Wabwino, kwaniritsa utumiki wako.

Paulo azindikira kuti imfa yake mpafupi. Aitana Timoteo amzonde. Mbiri ya Dema ndi ena

6 Pakuti ndilimkuthiridwa nsembe tsopano, ndipo nthawi ya kumasuka kwanga yafika.

7 Ndalimbana nako kulimbana kwabwino, ndatsiriza njirayo, ndasunga chikhulupiriro:

8 chotsalira wandiikira ine korona wa chilungamo, amene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa ine tsiku lijalo: ndipo si kwa ine ndekha, komatunso kwa onse amene anakonda maonekedwe ake.

9 Tayesetsa kudza kwa ine msanga:

10 pakuti Dema wandisiya ine, atakonda dziko lino lapansi, napita ku Tesalonika; Kresike ku Galatiya, Tito ku Dalamatiya.

11 Luka yekha ali pamodzi ndi ine. Umtenge Marko, adze pamodzi ndi iwe; pakuti ayenera kunditumikira.

12 Koma Tikiko ndamtuma ku Efeso.

13 Chofunda chija ndinachisiya ku Troasi kwa Karpo, udze nacho pakudza iwe, ndi mabuku, makamaka zikopa zija zolembedwa.

14 Aleksandro wosula mkuwa anandichitira zoipa zambiri: adzambwezera iye Ambuye monga mwa ntchito zake;

15 ameneyo iwenso uchenjere naye; pakuti anatsutsana nao mau athu.

16 Pa chodzikanira changa choyamba panalibe mmodzi anandithangata, koma onse anandisiya; chimenecho chisawerengedwe chowatsutsa.

17 Koma Ambuye anaima nane nandipatsa mphamvu; kuti mwa ine chilalikiro chimveke konsekonse, ndiamitunduonse amve; ndipo ndinalanditsidwa m’kamwa mwa mkango.

18 Ambuye adzandilanditsa ku ntchito yonse yoipa, nadzandipulumutsa ine kulowa Ufumu wake wa Kumwamba; kwa Iye ukhale ulemerero kunthawi za nthawi.Amen.

19 Pereka moni kwa Prisika ndi Akwila, ndi banja la Onesifore.

20 Erasto anakhalira mu Korinto; koma Trofimo ndamsiya wodwala ku Mileto.

21 Tayesetsa kudza isanadze nyengo yachisanu. Akukupatsa moni Yubulo, ndi Pude, ndi Lino, ndi Klaudia, ndi abale onse.

22 Ambuye akhale ndi mzimu wako. Chisomo chikhale nanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2TI/4-be63e4433deaf08f0df54ae0ced4d8e1.mp3?version_id=1068—

Categories
TITO

TITO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Tito sanali Myuda koma wa mitundu ina. Atatembenuka ndi kulowa mu mpingo, adasanduka mnzake wa Paulo womthandiza pa ntchito yolalikira, namuperekeza pa maulendo ake. Paulo adamsiya ku chilumba cha Krete kuti aziyang’anira mpingo kumeneko.

Pomulembera kalatayi, Paulo akumukumbutsa za makhalidwe oyenera atsogoleri a mpingo, makamaka ku Krete poti anthuwo mbiri yao sinali yabwino. Kenaka akumufotokozera kuti iye ayenera kuphunzitsira magulu ena a Akhristu: azibambo okalamba, amai okalamba (kuti iwonso aziphunzitsa amai achitsikana), achinyamata ndipo akapolo. Potsiriza Paulo alangiza Tito pa za mayendedwe a Chikhristu, kuti adziwe kuyanjanitsa anthu ndi kukopa mitima yao, apewe zilizonse zimene zingabweretse kukangana kapena kupatukana mu mpingo.

Za mkatimu

Mau oyamba 1.1-4

Za atsogoleri a mpingo 1.5-16

Ntchito yosamalira magulu osiyanasiyana mu mpingo 2.1-15

Malangizo ndi mau ena ochenjeza 3.1-11

Mau omaliza 3.12-15

Categories
TITO

TITO 1

1 Paulo, kapolo wa Mulungu, ndimtumwiwa YesuKhristu, monga mwa chikhulupiriro cha osankhika a Mulungu, ndi chizindikiritso cha choonadi chili monga mwa chipembedzo,

2 m’chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu, wosanamayo, analonjeza zisanayambe nthawi zosayamba;

3 koma pa nyengo za Iye yekha anaonetsa mau ake muulalikiro, umene anandisungitsa ine, monga mwa lamulo la Mpulumutsi wathu Mulungu:

4 kwa Tito, mwana wanga weniweni monga mwa chikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere za kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.

Asenzetsa Tito udindo wakusunga Mpingo wa ku Krete. Atsutsa aphunzitsi onyenga

5 Chifukwa cha ichi ndinakusiya iwe mu Krete, kuti ukalongosole zosowa, nukaike akulu m’midzi yonse, monga ndinakulamulira;

6 ngati wina ali wopanda chilema, mwamuna wa mkazi mmodzi, wokhala nao ana okhulupirira, wosasakaza zake, kapena wosakana kumvera mau.

7 Pakuti woyang’anira ayenera kukhala wopanda chilema, ngati mdindo wa Mulungu; wosati waliuma, wosapsa mtima msanga, wosati wachiwawa, wopanda ndeu, wosati wa chisiriro chonyansa;

8 komatu wokonda kuchereza alendo, wokonda zokoma, wodziweruza, wolungama, woyera mtima, wodziletsa;

9 wogwira mau okhulupirika monga mwa chiphunzitso, kuti akakhoze kuchenjeza m’chiphunzitso cholamitsa, ndi kutsutsa otsutsana naye.

10 Pakuti alipo ambiri osamvera mau, olankhula zopanda pake, ndi onyenga, makamaka iwo akumdulidwe,

11 amene ayenera kutsekedwa pakamwa; ndiwo amene apasula mabanja banja lonse, ndi kuphunzitsa zosayenera chifukwa cha chisiriro chonyansa.

12 Wina wa mwa iwo, ndiyemneneriwa iwo okha, anati, Akrete ndiwo amabodza masiku onse, zilombo zoipa, aumbombo, aulesi.

13 Umboni uwu uli woona. Mwa ichi uwadzudzule mokalipa, kuti akakhale olama m’chikhulupiriro,

14 osasamala nthano zachabe za Chiyuda, ndi malamulo a anthu opatuka kusiyana nacho choonadi.

15 Zonse ziyera kwa iwo amene ayera mtima; koma kwa iwo odetsedwa ndi osakhulupirira kulibe kanthu koyera; komatu zadetsedwa nzeru zao ndi chikumbumtima chao.

16 Avomereza kuti adziwa Mulungu, koma ndi ntchito zao amkana Iye, popeza ali onyansitsa, ndi osamvera, ndi pa ntchito zonse zabwino osatsimikizidwa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/TIT/1-e0ea9c6fabc561b7d3999df629e672ce.mp3?version_id=1068—

Categories
TITO

TITO 2

Machenjezedwe a okalamba ndi anyamata ndi akapolo. Akhale chitsanzo yekha Tito

1 Koma iwe, lankhula zimene ziyenera chiphunzitso cholamitsa:

2 okalamba akhale odzisunga, olemekezeka, odziletsa, olama m’chikhulupiriro, m’chikondi, m’chipiriro.

3 Momwemonso akazi okalamba akhale nao makhalidwe oyenera anthu oyera, osadierekeza, osakodwa nacho chikondi cha pavinyo, akuphunzitsa zokoma;

4 kuti akalangize akazi aang’ono akonde amuna ao, akonde ana ao,

5 akhale odziletsa, odekha, ochita m’nyumba mwao, okoma, akumvera amuna a iwo okha, kuti mau a Mulungu angachitidwe mwano.

6 Momwemonso anyamata uwadandaulire akhale odziletsa;

7 m’zonse udzionetsere wekha chitsanzo cha ntchito zabwino; m’chiphunzitso chako uonetsere chosavunda, ulemekezeko,

8 mau olama osatsutsika; kuti iye wakutsutsana achite manyazi, posakhala nako kanthu koipa kakutinenera ife.

9 Akapolo amvere ambuye ao a iwo okha, nawakondweretse m’zonse; osakana mau ao;

10 osatapa pa zao, komatu aonetsere chikhulupiriko chonse chabwino; kuti akakometsere chiphunzitso cha Mpulumutsi wathu Mulungu m’zinthu zonse.

11 Pakuti chaonekera chisomo cha Mulungu chakupulumutsa anthu onse,

12 ndi kutiphunzitsa ife kuti, pokana chisapembedzo ndi zilakolako za dziko lapansi, tikhale ndi moyo m’dziko lino odziletsa, ndi olungama, ndi opembedza;

13 akulindira chiyembekezo chodala, ndi maonekedwe a ulemerero wa Mulungu wamkulu ndi Mpulumutsi wathu YesuKhristu;

14 amene anadzipereka yekha m’malo mwa ife, kuti akatiombole ife kuzoipa zonse, nakadziyeretsere yekha anthu akhale ake enieni, achangu pa ntchito zokoma.

15 Izi lankhula, ndipo uchenjeze, nudzudzule ndi ulamuliro wonse. Munthu asakupeputse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/TIT/2-d63b8b5db3d7ce3073bd5a624611247e.mp3?version_id=1068—

Categories
TITO

TITO 3

1 Uwakumbutse iwo agonje kwa akulu, ndi aulamuliro, akhale omvera, okonzeka pa ntchito iliyonse yabwino;

2 asachitire mwano munthu aliyense, asakhale andeu, akhale aulere, naonetsere chifatso chonse pa anthu onse.

3 Pakuti kale ifenso tinali opusa, osamvera, onyengeka, akuchitira ukapolo zilakolako ndi zokondweretsa za mitundumitundu, okhala m’dumbo ndi njiru, odanidwa, odana wina ndi mnzake.

4 Koma pamene kukoma mtima, ndi chikondi cha pa anthu, cha Mpulumutsi wathu Mulungu zidanoneka,

5 zosati zochokera m’ntchito za m’chilungamo, zimene tidazichita ife, komatu monga mwa chifundo chake anatipulumutsa ife, mwa kutsuka kwa kubadwanso ndi makonzedwe a Mzimu Woyera,

6 amene anatsanulira pa ife mochulukira, mwa YesuKhristuMpulumutsi wathu;

7 kuti poyesedwa olungama ndi chisomo cha Iyetu, tikayesedwe olowa nyumba monga mwa chiyembekezo cha moyo wosatha.

8 Okhulupirika mauwa, ndipo za izi ndifuna kuti ulimbitse mau, kuti iwo akukhulupirira Mulungu asamalire akhalebe atsogoleri a ntchito zabwino. Izi nzokoma ndi zopindulitsa anthu;

9 koma pewa mafunso opusa, ndi mawerengedwe a mibadwo, ndi ndeu, ndi makani a pamalamulo; pakuti sizipindulitsa, ndipo zili zachabe.

10 Munthu wopatukira chikhulupiriro, utamchenjeza kamodzi ndi kawiri, umkanize,

11 podziwa kuti wotereyo wasandulika konse, nachimwa, nakhala wodzitsutsa yekha.

12 Pamene ndikatuma Aritema kwa iwe, kapena Tikiko, chita changu kudza kwa ine ku Nikopoli: pakuti ndatsimikiza mtima kugonerako nyengo yachisanu.

13 Zena nkhoswe ya milandu, ndi Apolo ufulumire kuwakonzera zaulendo, kuti asasowe kanthu,

14 Ndipo anthu athu aphunzirenso asunge ntchito zabwino zofunika, kuti asakhale osabala zipatso.

15 Akukupatsa moni onse akukhala pamodzi ndi ine. Pereka moni kwa otikondawo m’chikhulupiriro. Chisomo chikhale ndi inu nonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/TIT/3-cfcb0f893943058a29a045b40318586f.mp3?version_id=1068—

Categories
FILEMONI

FILEMONI Mau Oyamba

Mau Oyamba

Filemoni anali Mkhristu wodziwika bwino, makamaka mu mpingo wa ku Kolose. Iye anali ndi kapolo wake dzina lake Onesimo amene adamthawa. Tsiku lina Onesimoyo adakumana ndi Paulo, nthawi imeneyo nkuti Pauloyo ali m’ndende, ndipo kudzera mwa Pauloyo, Onesimo anasanduka Mkhristu. Paulo akumulembera kalata Filemoni uti amchitire chifundo kapolo wakeyo, ndipo amulandire ngati mbale wake mwa Khristu.

Za mkatimu

Mau oyamba 1.1-3

Ayamba wayamikira chikondi chake ndi chikhulupiriro chake 1.4-7

Paulo amnenera Onesimo 1.8-22

Mau omaliza 1.23-25

Categories
FILEMONI

FILEMONI 1

1 Paulo, wandende waKhristuYesu, ndi Timoteo mbaleyo, kwa Filemoni wokondedwayo ndi wantchito mnzathu,

2 ndi kwa Afiya mlongoyo, ndi Arkipo msilikali mnzathu, ndi kwaMpingouli m’nyumba yako:

3 Chisomo kwa inu ndi mtendere za kwa Mulungu Atate wathu ndi Ambuye Yesu Khristu.

4 Ndiyamika Mulungu wanga nthawi zonse, ndi kukumbukira iwe m’mapemphero anga,

5 pakumva za chikondi chako ndi chikhulupiriro uli nacho chakulinga kwa Ambuye Yesu, ndi kwa oyera mtima onse;

6 kuti chiyanjano cha chikhulupiriro chako chikakhale champhamvu podziwa chabwino chilichonse chili mwa inu, cha kwa Khristu.

7 Pakuti ndinali nacho chimwemwe chambiri ndi chisangalatso pa chikondi chako, popeza mitima ya oyera mtima yatsitsimuka mwa iwe, mbale.

Paulo apempherera kapolo wothawa wotembenuka mtima

8 Momwemo, ndingakhale ndili nako kulimbika mtima kwakukulu mu Khristu kukulamulira chimene chiyenera,

9 koma makamaka ndidandaulira mwa chikondi, pokhala wotere, Paulo nkhalamba, ndipo tsopano wandendenso wa Khristu Yesu;

10 ndikudandaulira chifukwa cha mwana wanga, amene ndambala m’ndende, Onesimo,

11 amene kale sanakupindulire, koma tsopano watipindulira bwino iwe ndi ine;

12 amene ndi yemweyo ndakubwezera iwe, ndiye mtima weniweni wa ine.

13 Ameneyo ndikadafuna ine kumsunga akhale nane, kuti m’malo mwako akadanditumikira ine m’ndende za Uthenga Wabwino:

14 koma wopanda kudziwa mtima wako sindinafune kuchita kanthu; kuti ubwino wako usakhale monga mokakamiza, komatu mwaufulu.

15 Pakuti kapena anasiyanitsidwa ndi iwe kanthawi chifukwa cha ichi, ndi kuti udzakhala naye nthawi zonse;

16 osatinso monga kapolo, koma woposa kapolo, mbale wokondedwa, makamaka ndi ine, koma koposa nanga ndi iwe, m’thupi, ndiponso mwa Ambuye.

17 Ngati tsono undiyesa woyanjana nawe, umlandire iye monga ine mwini.

18 Koma ngati anakulakwira kanthu, kapena wokongola kanthu, kanthu, kapena wakongola kanthu, undiwerengere ine kameneko;

19 ine Paulo ndichilemba ndi dzanja langa, ndidzachibwezera ine; kuti ndisanene nawe kuti iwe ndiwe mangawa anga.

20 Inde, mbale, ndikondwere nawe mwa Ambuye: utsitsimutse mtima wanga mwa Khristu.

21 Pokhulupirira kumvera kwako ndikulembera iwe, podziwa kuti udzachitanso koposa chimene ndinena.

22 Koma undikonzerenso pogona; pakuti ndiyembekeza kuti mwa mapemphero anu ndidzapatsidwa kwa inu.

23 Epafra wandende mnzanga mwa Khristu Yesu akukupatsa moni;

24 ateronso, Marko, Aristariko, Dema, Luka, antchito anzanga.

25 Chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu chikhale pamodzi ndi mzimu wanu.Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PHM/1-c1ff28ddda308b79f709697f9dd45fb2.mp3?version_id=1068—