Categories
AGALATIYA

AGALATIYA 2

1 Pamenepo popita zaka khumi ndi zinai ndinakweranso kunka kuYerusalemupamodzi ndi Barnabasi, ndinamtenganso Tito andiperekeze.

2 Koma ndinakwera kunkako movumbulutsa; ndipo ndinawauza Uthenga Wabwino umene ndiulalikira kwaamitundu; koma m’tseri kwa iwo omveka, kuti kapena ndingathamange, kapena ndikadathamanga chabe.

3 Komatu ngakhale Tito, amene anali ndi ine, ndiye Mgriki, sanamkakamize adulidwe;

4 ndicho chifukwa cha abale onyenga olowezedwa m’tseri, amene analowa m’tseri kudzazonda ufulu wathu umene tili nao mwaKhristuYesu, kuti akatichititse ukapolo.

5 Koma sitidawafumukire mowagonjera ngakhale ora limodzi; kuti choonadi cha Uthenga Wabwino chikhalebe ndi inu.

6 Koma iwo akuyesedwa ali kanthu (ngati anali otani kale, kulibe kanthu kwa ine; Mulungu salandira nkhope ya munthu) iwo omvekawo sanandionjezere ine kanthu;

7 koma pena, pakuona kuti anaikiza kwa ine Uthenga Wabwino wa kusadulidwa, monga kwa Petro Uthenga Wabwino wa mdulidwe

8 (pakuti Iye wakuchita mwa Petro kumtuma kwa odulidwa anachitanso mwa ine kundituma kwa amitundu);

9 ndipo pakuzindikira chisomocho chinapatsidwa kwa ine, Yakobo ndi Kefa ndi Yohane, amene anayesedwa mizati, anapatsa ine ndi Barnabasi dzanja lamanja la chiyanjano, kuti ife tipite kwa amitundu, ndi iwo kwa mdulidwe;

10 pokhapo kuti tikumbukire aumphawi; ndicho chomwe ndinafulumira kuchichita.

11 Koma pamene Kefa anadza ku Antiokeya ndinatsutsana naye pamaso pake, pakuti anatsutsika wolakwa.

12 Pakuti asanafike ena ochokera kwa Yakobo, anadya pamodzi ndi amitundu; koma atadza iwo, anadzibweza, ndi kudzipatula yekha, pakuopa iwo a ku mdulidwe.

13 Ndipo Ayuda otsala anawagwiranso m’maso pamodzi naye; kotero kuti Barnabasinso anatengedwa ndi kugwira m’maso kwao.

14 Komatu pamene ndinaona kuti sanalikuyenda koongoka, monga mwa choonadi cha Uthenga Wabwino, ndinati kwa Kefa pamaso pa onse, Ngati inu muli Myuda mutsata makhalidwe a amitundu, ndipo si a Ayuda, mukakamiza bwanji amitundu atsate makhalidwe a Ayuda?

15 Ife ndife Ayuda pachibadwidwe, ndipo sitili ochimwa a kwa amitundu;

16 koma podziwa kuti munthu sayesedwa wolungama pa ntchito ya lamulo, koma mwa chikhulupiriro cha Yesu Khristu, ifedi tinakhulupirira kwa Khristu Yesu, kuti tikayesedwe olungama ndi chikhulupiriro cha Khristu, ndipo si ndi ntchito za lamulo; pakuti palibe munthu adzayesedwa wolungama ndi ntchito za lamulo.

17 Koma ngati ife, pofuna kuyesedwa olungama mwa Khristu, tipezedwanso tili ochimwa tokha, kodi Khristu ali mtumiki wa uchimo chifukwa chake? Msatero ai.

18 Pakuti ngati izi zomwezi ndazigumula ndidzimanganso, ndidzitsimikizira ndekha ndili wolakwa.

19 Pakuti ine mwa lamulo ndafa kulamulo, kuti ndikhale ndi moyo kwa Mulungu.

20 Ndinapachikidwa ndi Khristu; koma ndili ndi moyo; wosatinso ine ai, koma Khristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndili nao tsopano m’thupi, ndili nao m’chikhulupiriro cha Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha chifukwa cha ine.

21 Sindichiyesa chopanda pake chisomo cha Mulungu; pakuti ngati chilungamo chili mwa lamulo, Khristu adafa chabe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GAL/2-385591379d34146934138156cddba972.mp3?version_id=1068—

Categories
AGALATIYA

AGALATIYA 3

Chilamulo sichingathe kupulumutsa; chititsogolera kutifikitsa kwa Khristu

1 Agalatiya opusa inu, anakulodzani ndani, inu amene YesuKhristuanaonetsedwa pamaso panu, wopachikidwa?

2 Ichi chokha ndifuna kuphunzira kwa inu, Kodi munalandira Mzimuyo ndi ntchito za lamulo, kapena ndi kumva kwa chikhulupiriro?

3 Kodi muli opusa otere? Popeza mudayamba ndi Mzimu, kodi tsopano mutsiriza ndi thupi?

4 Kodi mudamva zowawa zambiri zotere kwachabe? Ngatitu kwachabe.

5 Ndipo iye amene akuonjezerani inu Mzimuyo, nachita zimphamvu mwa inu, atero kodi ndi ntchito za lamulo, kapena ndi kumva kwa chikhulupiriro?

6 Monga Abrahamu anakhulupirira Mulungu, ndipo kunawerengedwa kwa iye chilungamo,

7 chotero zindikirani kuti iwo a chikhulupiriro ndiwo ana a Abrahamu.

8 Ndipo malembo, pakuoneratu kuti Mulungu adzayesa olungamaamitundundi chikhulupiriro, anayamba kale kulalikira Uthenga Wabwino kwa Abrahamu, kuti, Idzadalitsidwa mwa iwe mitundu yonse.

9 Kotero kuti iwo a chikhulupiriro adalitsidwa pamodzi ndi Abrahamu wokhulupirikayo.

10 Pakuti onse amene atama ntchito za lamulo liwakhalira temberero; pakuti kwalembedwa,

Wotembereredwa aliyense

wosakhala m’zonse zolembedwa

m’buku la chilamulo, kuzichita izi.

11 Ndipo chidziwikatu kuti palibe munthu ayesedwa wolungama ndi lamulo pamaso pa Mulungu; pakuti, Wolungama adzakhala ndi moyo ndi chikhulupiriro;

12 koma chilamulo sichichokera kuchikhulupiriro; koma, Wakuzichita izi adzakhala ndi moyo ndi izi.

13 Khristu anatiombola ku temberero la chilamulo, atakhala temberero m’malo mwathu; pakuti kwalembedwa,

Wotembereredwa aliyense wopachikidwa pamtengo.

14 Kuti dalitso la Abrahamu mwa Khristu Yesu, lichitike kwa amitundu; kuti tikalandire lonjezano la Mzimuyo, mwa chikhulupiriro.

15 Abale, ndinena monga munthu. Pangano, lingakhale la munthu, litalunzika, palibe munthu aliyesa chabe, kapena kuonjezapo.

16 Ndipo malonjezano ananenedwa kwa Abrahamu ndi kwa mbeu yake. Sanena, Ndipo kwa zimbeu, ngati kunena zambiri; komatu ngati kunena imodzi, Ndipo kwa mbeu yako, ndiye Khristu.

17 Ndipo ichi ndinena: Lamulo, limene linafika zitapita zaka mazana anai mphambu makumi atatu, silifafaniza pangano lolunzika kale ndi Mulungu, kuliyesa lonjezanolo lachabe.

18 Pakuti ngati kulowa nyumba kuchokera kulamulo, sikuchokeranso kulonjezano; koma kumeneku Mulungu anampatsa Abrahamu kwaufulu mwa lonjezano.

19 Nanga chilamulo tsono? Chinaonjezeka chifukwa cha zolakwa, kufikira ikadza mbeu imene adailonjezera; ndipo chinakonzeka ndiangelom’dzanja la nkhoswe.

20 Koma nkhoswe siili ya mmodzi; koma Mulungu ali mmodzi.

21 Pamenepo kodi chilamulo chitsutsana nao malonjezano a Mulungu? Msatero ai. Pakuti chikadapatsidwa chilamulo chakukhoza kuchitira moyo, chilungamo chikadachokera ndithu kulamulo.

22 Komatu lembo linatsekereza zonse pansi pa uchimo, kuti lonjezano la kwa chikhulupiriro cha Yesu Khristu likapatsidwe kwa okhulupirirawo.

23 Koma chisanadze chikhulupiriro tinasungidwa pomvera lamulo otsekedwa kufikira chikhulupiriro chimene chikavumbulutsidwa bwinobwino.

24 Momwemo chilamulo chidakhala namkungwi wathu wakutifikitsa kwa Khristu, kuti tikayesedwe olungama ndi chikhulupiriro.

25 Koma popeza chadza chikhulupiriro, sitikhalanso omvera namkungwi.

26 Pakuti inu nonse muli ana a Mulungu, mwa chikhulupiriro cha mwa Khristu Yesu.

27 Pakuti nonse amene munabatizidwa kwa Khristu mudavala Khristu.

28 Muno mulibe Myuda, kapena Mgriki, muno mulibe kapolo, kapena mfulu, muno mulibe mwamuna ndi mkazi; pakuti muli nonse mmodzi mwa Khristu Yesu.

29 Koma ngati muli a Khristu, muli mbeu ya Abrahamu, nyumba monga mwa lonjezano.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GAL/3-93bca78fb47160ab321381a8bdc8b7c3.mp3?version_id=1068—

Categories
AGALATIYA

AGALATIYA 4

Uthenga Wabwino utimasula kuchilamulo

1 Koma ndinena kuti, pokhala wolowa nyumba ali wakhanda, sasiyana ndi kapolo, angakhale ali mwini zonse;

2 komatu ali wakumvera omsungira ndi adindo, kufikira nthawi yoikika kale ndi atate wake.

3 Koteronso ife, pamene tinali akhanda, tinali akapolo akumvera miyambo ya dziko lapansi;

4 koma pokwaniridwa nthawi, Mulungu anatuma Mwana wake, wobadwa ndi mkazi, wobadwa wakumvera lamulo,

5 kuti akaombole iwo akumvera lamulo, kuti ife tikalandire umwana.

6 Ndipo popeza muli ana, Mulungu anatumiza Mzimu wa Mwana wake alowe m’mitima yathu, wofuulaAbba!Atate!

7 Kotero kuti sulinso kapolo, koma mwana; koma ngati mwana, wolowa nyumbanso mwa Mulungu.

8 Komatu pajapo, posadziwa Mulungu inu, munachitira ukapolo iyo yosakhala milungu m’chibadwidwe chao;

9 koma tsopano, podziwa Mulungu inu, koma makamaka podziwika ndi Mulungu, mubwereranso bwanji kutsata miyambo yofooka ndi yaumphawi, imene mufuna kubwerezanso kuichitira ukapolo?

10 Musunga masiku, ndi miyezi, ndi nyengo, ndi zaka.

11 Ndiopera inu, kuti kapena ndadzivutitsa ndi inu chabe.

12 Abale, ndikupemphani, khalani monga ine, pakuti inenso ndili monga inu. Simunandichitire choipa ine;

13 koma mudziwa kuti m’kufooka kwa thupi ndinakulalikirani Uthenga Wabwino poyamba:

14 ndipo chija cha m’thupi langa chakukuyesani inu simunachipeputse, kapena sichinakunyansireni, komatu munandilandira ine mongamngelowa Mulungu, mongaKhristuYesu mwini.

15 Pamenepo thamo lanu lili kuti? Pakuti ndikuchitirani inu umboni, kuti, kukadatheka, mukadakolowola maso anu ndi kundipatsa ine.

16 Kotero kodi ndasanduka mdani wanu, pakukunenerani zoona?

17 Achita changu pa inu koma si kokoma ai, komatu afuna kukutsekerezani inu kunja, kuti mukawachitire iwowa changu.

18 Koma nkwabwino kuchita changu m’zabwino nthawi zonse, si pokhapokha pokhala nanu pamodzi ine.

19 Tiana tanga, amene ndilikumvanso zowawa za kubala inu, kufikira Khristu aumbika mwa inu,

20 koma mwenzi nditakhala nanu tsopano, ndi kusintha mau anga; chifukwa ndisinkhasinkha nanu.

Sara ndi Hagara atifanizira mapangano awiriwo

21 Ndiuzeni, inu akufuna kukhala omvera lamulo, kodi simukumva chilamulo?

22 Pakuti palembedwa, kuti Abrahamu anali nao ana aamuna awiri, mmodzi wobadwa mwa mdzakazi, ndi mmodzi wobadwa mwa mfulu.

23 Komatu uyo wa mdzakazi anabadwa monga mwa thupi; koma iye wa mfuluyo, anabadwa monga mwa lonjezano. Izo ndizo zophiphiritsa;

24 pakuti akaziwa ali mapangano awiri, mmodzi wa kuphiri la Sinai, akubalira ukapolo, ndiye Hagara.

25 Koma Hagara ndiye phiri la Sinai, mu Arabiya, nafanana ndiYerusalemuwa tsopano; pakuti ali muukapolo pamodzi ndi ana ake.

26 Koma Yerusalemu wa kumwamba uli waufulu, ndiwo amai wathu.

27 Pakuti kwalembedwa,

Kondwera, chumba iwe wosabala;

imba nthungululu, nufuule iwe wosamva kuwawa kwa kubala;

pakuti ana ake a iye ali mbeta achuluka

koposa ana a iye ali naye mwamuna.

28 Koma ife, abale, monga Isaki, tili ana a lonjezano.

29 Komatu monga pompaja iye wobadwa monga mwa thupi anazunza wobadwa monga mwa Mzimu, momwemonso tsopano.

30 Koma lembo linena chiyani? Taya kubwalo mdzakazi ndi mwana wake, pakuti sadzalowa nyumba mwana wa mdzakazi pamodzi ndi mwana wa mfulu.

31 Chifukwa chake, abale, sitili ana a mdzakazi, komatu a mfulu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GAL/4-08a091e377d42d53ad74a50678e5b0ac.mp3?version_id=1068—

Categories
AGALATIYA

AGALATIYA 5

Asunge ufulu wa Chikhristu

1 Khristuanatisandutsa mfulu, kuti tikhale mfulu; chifukwa chake chilimikani, musakodwenso ndi goli la ukapolo.

2 Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Khristu simudzapindula naye kanthu.

3 Ndichitanso umboni kwa munthu yense wolola amdule, kuti ali wamangawa kuchita chilamulo chonse.

4 Mulibe kanthu ndi Khristu, inu amene muyesedwa olungama ndi lamulo; mudagwa posiyana nacho chisomo.

5 Pakuti ife mwa Mzimu, kuchokera m’chikhulupiriro, tilindira chiyembekezo cha chilungamo.

6 Pakuti mwa Khristu Yesu kapenamdulidwekapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu chikhulupiriro, chakuchititsa mwa chikondi.

7 Munathamanga bwino; anakuletsani ndani kuti musamvere choonadi?

8 Kukopa kumene sikuchokera kwa Iye anakuitanani.

9 Chotupitsa pang’ono chitupitsa mtanda wonse.

10 Ine ndikhulupirira inu mwa Ambuye, kuti simudzakhala nao mtima wina; koma iye wakuvuta inu, angakhale ali yani, adzasenza chitsutso chake.

11 Koma ine, abale, ngati ndilalikiranso mdulidwe, ndizunzikanso bwanji? Pamenepo chikhumudwitso cha mtanda chidatha.

12 Mwenzi atadzidula, iwo akugwedezetsani inu.

13 Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; chokhacho musachite nao ufulu wanu chothandizira thupi, komatu mwachikondi chitiranani ukapolo.

14 Pakuti mau amodzi akwaniritsa chilamulo chonse ndiwo; Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.

15 Koma ngati mulumana ndi kudyana, chenjerani mungaonongane.

Ntchito za thupi ndi zipatso za Mzimu

16 Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse chilakolako cha thupi.

17 Pakuti thupi lilakalaka potsutsana naye Mzimu, ndi Mzimu potsutsana nalo thupi; pakuti izi sizilingana; kuti zimene muzifuna musazichite.

18 Ngati Mzimu akutsogolerani, simuli omvera lamulo.

19 Ndipo ntchito za thupi zionekera, ndizo dama, chodetsa, kukhumba zonyansa,

20 kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,

21 njiru, kuledzera, mchezo, ndi zina zotere; zimene ndikuchenjezani nazo, monga ndachita, kuti iwo akuchitachita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

22 Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,

23 chifatso, chiletso; pokana zimenezi palibe lamulo.

24 Koma iwo a Khristu Yesu adapachika thupi, ndi zokhumba zake, ndi zilakolako zake.

25 Ngati tili ndi moyo ndi Mzimu, ndi Mzimunso tiyende.

26 Tisakhale odzikuza, outsana, akuchitirana njiru.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GAL/5-6874a9a58b60e6c51c47ab4708aedf46.mp3?version_id=1068—

Categories
AGALATIYA

AGALATIYA 6

Malangizo otsiriza, kulawirana

1 Abale, ngatinso munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu, mubweze wotereyo mu mzimu wa chifatso; ndi kudzipenyerera wekha, ungayesedwe nawenso.

2 Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mufitse chilamulo chaKhristu.

3 Pakuti ngati wina ayesa ali kanthu pokhala ali chabe, adzinyenga yekha.

4 Koma yense ayesere ntchito yake ya iye yekha, ndipo pamenepo adzakhala nako kudzitamandira chifukwa cha iye yekha, si chifukwa cha wina.

5 Pakuti yense adzasenza katundu wake wa iye mwini.

6 Koma iye amene aphunzira mau, ayenera kuchereza womphunzitsayo m’zonse zabwino.

7 Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti chimene munthu achifesa, chimenenso adzachituta.

8 Pakuti wakufesera kwa thupi la iye yekha, chochokera m’thupi adzatuta chivundi; koma wakufesera kwa Mzimu, chochokera mu Mzimu adzatuta moyo wosatha.

9 Koma tisaleme pakuchita zabwino; pakuti pa nyengo yake tidzatuta tikapanda kufooka.

10 Chifukwa chake, monga tili nayo nyengo, tichitire onse chokoma, koma makamaka iwo a pa banja la chikhulupiriro.

11 Taonani, malembedwe aakuluwo ndakulemberani inu ndi dzanja langa la ine mwini.

12 Onse amene afuna kuonekera okoma m’thupi, iwowa akukakamizani inu mudulidwe; chokhacho, chakuti angazunzike chifukwa cha mtanda wa Khristu.

13 Pakuti angakhale iwo omwe odulidwa sasunga lamulo; komatu afuna inu mudulidwe, kuti akadzitamandire m’thupi lanu.

14 Koma kudzitamandira ine konsekonse, iai, koma mu mtanda wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene mwa Iye dziko lapansi lapachikidwira ine, ndi ine ndapachikidwira dziko lapansi.

15 Pakuti mdulidwe ulibe kanthu, kusadulidwa kulibe kanthunso, komatu wolengedwa watsopano.

16 Ndipo onse amene atsata chilangizo ichi, mtendere ndi chifundo zikhale pa iwo, ndi pa Israele wa Mulungu.

17 Kuyambira tsopano palibe munthu andivute, pakuti ndili nayo ine m’thupi mwanga mikwingwirima ya Yesu.

18 Chisomo cha Ambuye wathu Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu, abale.Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/GAL/6-33f06d7807d214f1000b3d38fa06dd0c.mp3?version_id=1068—

Categories
AEFESO

AEFESO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Kalata ya Paulo mtumwi yolembera kwa Aefeso

ikunena za “makonzedwe a Mulungu…ndi makwaniridwe a nyengozo, akasonkhanitse pamodzi zonse mwa Khristu, za kumwamba, ndi za padziko”. (1.10) Kalatayi ndi pempho kwa anthu a Mulungu kuti akhale molingana ndi chikonzero chachikuluchi pofuna kuyanjanitsa mtundu wonse wa anthu kudzera mu umodzi umene upezeka mwa Yesu Khristu.

Mu gawo loyamba la buku la

Aefeso

wolembayo akutambasula mutu wa umodzi wa mpingo pamene akukamba za m’mene Mulungu Atate anasankhira anthu ake, ndipo m’mene iwowo amalandira chikhululukiro cha machimo namasulidwa kuchokera kumachimo kudzera mwa Mwana wake Yesu Khristu. Komanso akukamba za lonjezo lalikulu la Mulungu limene litsimikizidwa ndi Mzimu Woyera. Mu gawo lachiwiri iye akuwadandaulira awerengi ake kuti umodzi wao mwa Khristu uwonekere poyera pa mayendedwe ao ndi pa moyo wao wonse.

M’kalatamu akugwiritsa ntchito zifanizo zingapo pofuna kuonetsa umodzi wa anthu a Mulungu mwa Khristu: mpingo uli ngati thupi, ndipo Khristu ali ngati mutu wake; kapenanso ngati nyumba, ndipo Khristu ndiye mwala wokhala pangodya; kapenanso ngati mkazi, ndipo Khristu ndiye mwamuna wake wa mpingo. Kenaka kalatayi ikufotokoza zinthu zinanso zofunikira pamene wolembayo akunena za chisomo cha Mulungu mwa Khristu. Chilichonse chikuyesedwa molingana ndi chikondi, kudzipereka, kukhululukira machimo, chisomo komanso chiyero cha Khristu.

Za mkatimu

Mau oyamba 1.1-2

Khristu ndi mpingo 1.3—3.21

Moyo watsopano mwa Khristu 4.1—6.20

Mau omaliza 6.21-24

Categories
AEFESO

AEFESO 1

1 Paulo,mtumwiwaKhristuYesu, mwa chifuniro cha Mulungu, kwa oyera mtima amene ali mu Efeso, ndi kwa iwo okhulupirika mwa Khristu Yesu:

2 Chisomo kwa inu, ndi mtendere wochokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Khristu.

Madalitso a Mulungu mwa Yesu Khristu, Mpulumutsi wathu ndi mutu wa Mpingo

3 Wolemekezeka Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene anatidalitsa ife ndi dalitso lonse la mzimu m’zakumwamba mwa Khristu;

4 monga anatisankha ife mwa Iye, lisanakhazikike dziko lapansi, tikhale ife oyera mtima, ndi opanda chilema pamaso pake m’chikondi.

5 Anatikonzeratu tilandiridwe ngati ana a Iye yekha mwa Yesu Khristu, monga umo kunakomera chifuniro chake,

6 kuti uyamikidwe ulemerero wa chisomo chake, chimene anatichitira ife kwaufulu mwa Wokondedwayo.

7 Tili ndi maomboledwe mwa mwazi wake, chikhululukiro cha zochimwa, monga mwa kulemera kwa chisomo chake,

8 chimene anatichulukitsira ife m’nzeru zonse, ndi chisamaliro.

9 Anatizindikiritsa ife chinsinsi cha chifuniro chake, monga kunamkomera ndi monga anatsimikiza mtima kale mwa Iye,

10 kuti pa makonzedwe a makwaniridwe a nyengozo, akasonkhanitse pamodzi zonse mwa Khristu, za kumwamba, ndi za padziko.

11 Mwa Iye tinayesedwa akeake olandira cholowa, popeza tinakonzekeratu monga mwa chitsimikizo mtima cha Iye wakuchita zonse monga mwa uphungu wa chifuniro chake;

12 kuti ife amene tinakhulupirira Khristu kale tikayamikitse ulemerero wake.

13 Mwa Iyeyo inunso, mutamva mau a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, ndi kumkhulupirira Iye, munasindikizidwa chizindikiro ndi Mzimu Woyera wa lonjezano,

14 ndiye chikole cha cholowa chathu, kuti akeake akaomboledwe, ndi kuti ulemerero wake uyamikike.

15 Mwa ichi inenso, m’mene ndamva za chikhulupiriro cha mwa Ambuye Yesu chili mwa inu ndi chikondi chanu, chimenenso mufikitsira oyera mtima onse,

16 sindileka kuyamika chifukwa cha inu, ndi kukumbukira inu m’mapemphero anga;

17 kuti Mulungu wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa ulemerero, akupatseni inu mzimu wa nzeru, ndi wa vumbulutso kuti mukamzindikire Iye;

18 ndiko kunena kuti maso a mitima yanu awalitsike, kuti mukadziwe inu chiyembekezo cha kuitana kwake nchiyani; chiyaninso chuma cha ulemerero wa cholowa chake mwa oyera mtima,

19 ndi chiyani ukulu woposa wa mphamvu yake ya kwa ife okhulupirira, monga mwa machitidwe a mphamvu yake yolimba,

20 imene anachititsa mwa Khristu, m’mene anamuukitsa kwa akufa, namkhazikitsa padzanja lake lamanja m’zakumwamba,

21 pamwamba pa ukulu wonse, ndi ulamuliro, ndi mphamvu, ndi ufumu, ndi dzina lililonse lotchedwa, si m’nyengo ino ya pansi pano yokha, komanso mwa iyo ikudza;

22 ndipo anakonza zonse pansi pa mapazi ake, nampatsa Iye akhale mutu pamutu pa zonse, kwaMpingo

23 amene ali thupi lake, mdzazidwe wa Iye amene adzaza zonse m’zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EPH/1-3c3dca73d1be39222c9363ebbc1a6fcb.mp3?version_id=1068—

Categories
AEFESO

AEFESO 2

Chipulumutso chichokera kuchisomo

1 Ndipo inu, anakupatsani moyo, pokhala munali akufa ndi zolakwa, ndi zochimwa zanu,

2 zimene munayendamo kale, monga mwa mayendedwe a dziko lapansi lino, monga mwa mkulu wa ulamuliro wa mlengalenga, wa mzimu wakuchita tsopano mwa ana a kusamvera;

3 amene ife tonsenso tinagonera pakati pao kale, m’zilakolako za thupi lathu, ndi kuchita zifuniro za thupi, ndi za maganizo, ndipo tinali ana a mkwiyo chibadwire, monganso otsalawo;

4 koma Mulungu, wolemera chifundo, chifukwa cha chikondi chake chachikulu chimene anatikonda nacho,

5 tingakhale tinali akufa m’zolakwa zathu, anatipatsa moyo pamodzi ndiKhristu(muli opulumutsidwa ndi chisomo),

6 ndipo anatiukitsa pamodzi, natikhazikitsa pamodzi m’zakumwamba mwaKhristuYesu;

7 kuti akaonetsere m’nthawi zilinkudza chuma choposa cha chisomo chake, m’kukoma mtima kwa pa ife mwa Khristu Yesu.

8 Pakuti muli opulumutsidwa ndi chisomo chakuchita mwa chikhulupiriro, ndipo ichi chosachokera kwa inu: chili mphatso ya Mulungu;

9 chosachokera kuntchito, kuti asadzitamandire munthu aliyense.

10 Pakuti ife ndife chipango chake, olengedwa mwa Khristu Yesu, kuchita ntchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m’menemo.

Ayuda ndi amitundu ayanjanitsidwa ndi Mulungu mwa mtanda wa Khristu

11 Momwemo kumbukirani, kuti kale inuamitundum’thupi, otchedwa kusadulidwa ndi iwo otchedwamdulidwem’thupi, umene udachitika ndi manja;

12 kuti nthawi ija munali opanda Khristu, alendo a padera ndi mbumba ya Israele, ndi alendo alibe kanthu ndi mapangano a malonjezano, opanda chiyembekezo, ndi opanda Mulungu m’dziko lapansi.

13 Koma tsopano mwa Khristu Yesu inu amene munali kutali kale, anakusendezani mukhale pafupi m’mwazi wa Khristu.

14 Pakuti Iye ndiye mtendere wathu, amene anachita kuti onse awiri akhale mmodzi, nagumula khoma lakudulitsa pakati,

15 atachotsa udani m’thupi lake, ndiwo mau a chilamulo cha kutchulako malangizo; kuti alenge awiriwa mwa Iye yekha, akhale munthu mmodzi watsopano, ndi kuchitapo mtendere;

16 ndi kuti akayanjanitse awiriwa ndi Mulungu, m’thupi limodzi mwa mtandawo, atapha nao udaniwo;

17 ndipo m’mene anadza, analalikira Uthenga Wabwino wa mtendere kwa inu akutali, ndi mtendere kwa iwo apafupi;

18 kuti mwa Iye ife tonse awiri tili nao malowedwe athu kwa Atate, mwa Mzimu mmodzi.

19 Pamenepo ndipo simulinso alendo ndi ogonera, komatu muli a mudzi womwewo wa oyera mtima ndi a banja la Mulungu;

20 omangika pa maziko aatumwindi aneneri, pali Khristu Yesu mwini, mwala wa pangodya;

21 mwa Iye chimango chonse cholumikizika pamodzi bwino, chikula, chikhale Kachisi wopatulika mwa Ambuye;

22 chimene inunso mumangidwamo pamodzi, mukhale chokhalamo Mulungu mwa Mzimu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EPH/2-054984f16af14989be1bea8f545f37dd.mp3?version_id=1068—

Categories
AEFESO

AEFESO 3

Chinsinsi cha maitanidwe a amitundu

1 Chifukwa cha ichi ine Paulo, ndine wandende waKhristuYesu chifukwa cha inuamitundu,

2 ngatitu munamva za udindo wa chisomo cha Mulungu chimene anandipatsa ine cha kwa inu;

3 ndi umo anandizindikiritsa chinsinsicho mwa vumbulutso, monga ndinalemba kale mwachidule,

4 chimene mukhoza kuzindikira nacho, pakuchiwerenga, chidziwitso changa m’chinsinsi cha Khristu,

5 chimene sanachizindikiritse ana a anthu m’mibadwo ina, monga anachivumbulutsa tsopano kwaatumwindi aneneri ake oyera mwa Mzimu,

6 kuti amitundu ali olowa nyumba pamodzi ndi ife, ndi ziwalo zinzathu za thupilo, ndi olandira nafe pamodzi palonjezano mwa Khristu Yesu, mwa Uthenga Wabwino,

7 umene anandikhalitsa mtumiki wake monga mwa mphatso ya chisomo cha Mulungu, chimene anandipatsa ine, monga mwa machitidwe a mphamvu yake.

8 Kwa ine wochepa ndi wochepetsa wa onse oyera mtima anandipatsa chisomo ichi ndilalikire kwa amitundu chuma chosalondoleka cha Khristu;

9 ndi kuwalitsira onse adziwe makonzedwe a chinsinsicho, chimene chinabisika kuyambira kalekale mwa Mulungu wolenga zonse;

10 kuti muMpingoazindikiritse tsopano kwa akulu ndi maulamuliro m’zakumwamba nzeru ya mitundumitundu ya Mulungu,

11 monga mwa chitsimikizo mtima cha nthawi za nthawi, chimene anachita mwa Khristu Yesu Ambuye wathu:

12 amene tili naye chokhazikika mtima ndi chiyandiko cholimbika, mwa chikhulupiriro cha pa Iye.

13 Mwa ichi ndipempha kuti musade mtima m’zisautso zanga chifukwa cha inu, ndiwo ulemerero wanu.

Paulo apempherera Aefeso

14 Chifukwa cha ichi ndipinda maondo anga kwa Atate,

15 amene kuchokera kwa Iye fuko lonse la m’mwamba ndi la padziko alitcha dzina,

16 kuti monga mwa chuma cha ulemerero wake akulimbikitseni inu ndi mphamvu mwa Mzimu wake, m’kati mwanu,

17 kuti Khristu akhale chikhalire mwa chikhulupiriro m’mitima yanu; kuti, ozika mizu ndi otsendereka m’chikondi,

18 mukakhozetu kuzindikira pamodzi ndi oyera mtima onse, kupingasa, ndi utali, ndi kukwera,

19 ndi kuzama nchiyani; ndi kuzindikira chikondi cha Khristu, chakuposa mazindikiridwe, kuti mukadzazidwe kufikira chidzalo chonse cha Mulungu.

20 Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife,

21 kwa Iye ukhale ulemerero mu Mpingo ndi mwa Khristu Yesu, kufikira mibadwo yonse ya nthawi za nthawi.Amen.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EPH/3-a8dfaafbab123e39e8f3ddd04857eb2e.mp3?version_id=1068—

Categories
AEFESO

AEFESO 4

Umodzi wa iwo a chikhulupiriro

1 Ndikudandaulirani inu tsono, ine wandende mwa Ambuye, muyende koyenera maitanidwe amene munaitanidwa nao,

2 ndi kuonetsera kudzichepetsa konse, ndi chifatso, ndi kuonetsera chipiriro, ndi kulolerana wina ndi mnzake, mwa chikondi;

3 ndi kusamalitsa kusunga umodzi wa Mzimu mwa chimangiriro cha mtendere.

4 Thupi limodzi ndi Mzimu mmodzi, monganso anakuitanani m’chiyembekezo chimodzi cha maitanidwe anu;

5 Ambuye mmodzi, chikhulupiriro chimodzi, ubatizo umodzi,

6 Mulungu mmodzi ndi Atate wa onse amene ali pamwamba pa onse, ndi mwa onse, ndi m’kati mwa zonse.

7 Ndipo kwa yense wa ife chapatsika chisomo, monga mwa muyeso wa mphatso yaKhristu.

8 Chifukwa chake anena,

M’mene anakwera kumwamba, anamanga ndende undende,

naninkha zaufulu kwa anthu.

9 Koma ichi, chakuti, Anakwera, nchiyani nanga koma kuti anatsikiranso ku madera a kunsi kwa dziko?

10 Iye wotsikayo ndiye yemweyonso anakwera, popitiriratu miyamba yonse, kuti akadzaze zinthu zonse.

11 Ndipo Iye anapatsa ena akhaleatumwi; ndi ena aneneri; ndi ena alaliki; ndi ena abusa, ndi ena aphunzitsi;

12 kuti akonzere oyera mtima kuntchito ya utumiki, kumangirira thupi la Khristu;

13 kufikira ife tonse tikafikira ku umodzi wa chikhulupiriro, ndi wa chizindikiritso cha Mwana wa Mulungu, kwa munthu wangwiro, ku muyeso wa msinkhu wa chidzalo cha Khristu.

14 Kuti tisakhalenso makanda, ogwedezekagwedezeka, natengekatengeka ndi mphepo yonse ya chiphunzitso, ndi tsenga la anthu, ndi kuchenjerera kukatsata chinyengo cha kusocheretsa;

15 koma ndi kuchita zoona mwa chikondi tikakule m’zinthu zonse, kufikira Iye amene ali mutu ndiye Khristu;

16 kuchokera mwa Iye thupi lonse, lolukidwa ndi lolumikizidwa pamodzi, pothandizanapo mfundo yonse, monga mwa kuchititsa kwa chiwalo chonse pa muyeso wake, lichita makulidwe a thupi, kufikira chimango chake mwa chikondi.

Kusiyana kwa kuyera mtima kwa Chikhristu ndi mayendedwe oipa a akunja

17 Pamenepo ndinena ichi, ndipo ndichita umboni mwa Ambuye, kuti simuyendanso inu mongansoamitunduangoyenda, m’chitsiru cha mtima wao,

18 odetsedwa m’nzeru zao, oyesedwa alendo pa moyo wa Mulungu, chifukwa cha chipulukiro chili mwa iwo, chifukwa cha kuumitsa kwa mitima yao;

19 amenewo popeza sazindikiranso kanthu konse, anadzipereka okha kuti akhumbe zonyansa, kuti achite chidetso chonse mu umbombo.

20 Koma inu simunaphunzire Khristu chotero,

21 ngatitu mudamva Iye, ndipo munaphunzitsidwa mwa Iye, monga choonadi chili mwa Yesu;

22 kuti muvule, kunena za makhalidwe anu oyamba, munthu wakale, wovunda potsata zilakolako za chinyengo;

23 koma kuti mukonzeke, mukhale atsopano mu mzimu wa mtima wanu,

24 nimuvale munthu watsopano, amene analengedwa monga mwa Mulungu, m’chilungamo, ndi m’chiyero cha choonadi.

25 Mwa ichi, mutataya zonama, lankhulani zoona yense ndi mnzake; pakuti tili ziwalo wina ndi mnzake.

26 Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,

27 ndiponso musampatse malo mdierekezi.

28 Wakubayo asabenso; koma makamaka agwiritse ntchito, nagwire ntchito yokoma ndi manja ake, kuti akhale nacho chakuchereza wosowa.

29 Nkhani yonse yovunda isatuluke m’kamwa mwanu, koma ngati pali ina yabwino kukumangirira monga mofunika ndiyo, kuti ipatse chisomo kwa iwo akumva.

30 Ndipo musamvetse chisoni Mzimu Woyera wa Mulungu, amene munasindikizidwa chizindikiro mwa Iye, kufikira tsiku la maomboledwe.

31 Chiwawo chonse, ndi kupsa mtima, ndi mkwiyo, ndi chiwawa, ndi mwano zichotsedwe kwa inu, ndiponso choipa chonse.

32 Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzake, a mtima wachifundo, akukhululukirana nokha, monganso Mulungu mwa Khristu anakhululukira inu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EPH/4-257090310aea5a1baec5e980b2138c2f.mp3?version_id=1068—