Achenjezedwa kuti adani adzamangira Yerusalemu misasa
1 Ananu a Benjamini, pulumukani pothawa pakati paYerusalemu, ombani lipenga mu Tekowa, kwezani chizindikiro mu Betehakeremu; pakuti chaoneka choipa chotuluka m’mpoto ndi kuononga kwakukulu.
2 Ndidzachotsa mwana wamkazi waZiyonimkazi wokoma ndi wololopoka.
3 Abusa ndi nkhosa zao adzadza kwa iye; adzamanga mahema ao pomzinga iye; adzadya yense pokhala pake.
4 Lalikirani nkhondo yakumenyana ndi iye; ukani, tikwere pakati pa usana. Tsoka kwa ife! Pakuti dzuwa lapendeka, mithunzi ya madzulo yatambasuka.
5 Ukani, tiyende usiku, tipasule nyumba zake.
6 Pakuti Yehova wa makamu atero, Dulani mitengo, unjikani nthumbira pomenyana ndi Yerusalemu; mzinda wakudzalangidwa ndi uwu; m’kati mwake modzala nsautso.
7 Monga kasupe atulutsa madzi ake, chomwecho atulutsa zoipa zake; chiwawa ndi kufunkha zimveka m’kati mwake; pamaso panga masiku onse pali kulira ndi mabala.
8 Ulangizidwe, Yerusalemu, ungakuchokere moyo wanga, ndingakuyese iwe bwinja, dziko losakhalamo anthu.
9 Yehova wa makamu atero, Adzakunkha otsalira a Israele monga mpesa; bweza dzanja lako monga wakutchera mphesa m’madengu ake.
10 Ndidzanena ndi yani, ndidzachita mboni kwa yani, kuti amve? Taona khutu lao lili losadulidwa, ndipo sangathe kumva; taona, mau a Yehova awatonzetsa iwo; sakondwera nao.
11 Chifukwa chake ndadzala ndi ukali wa Yehova; ndalema ndi kudzikaniza; tsanulirani pa ana a pabwalo, ndi pa misonkhano ya anyamata, pakuti ngakhale mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, okalamba ndi iye amene achuluka masiku ake.
12 Nyumba zao zidzasanduka za ena, pamodzi ndi minda yao ndi akazi ao; pakuti ndidzatambasula dzanja langa pa okhala m’dziko, ati Yehova.
13 Pakuti kuyambira wamng’ono kufikira wamkulu onse akhala akusirira; ndiponso kuyambiramnenerikufikira wansembe onse achita monyenga.
14 Ndiponso apoletsa bala la anthu anga pang’onong’ono, ndi kuti, Mtendere, mtendere; koma palibe mtendere.
15 Kodi anakhala ndi manyazi pamene anachita chonyansa? Iai, sanakhale konse ndi manyazi, sanathe kunyala; chifukwa chake adzagwa mwa iwo akugwa; panthawi pamene ndidzafika kwa iwo, adzagwetsedwa, ati Yehova.
16 Yehova atero, Imani m’njira ndi kuona, funsani za mayendedwe akale, m’menemo muli njira yabwino, muyende m’menemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu; koma anati, Sitidzayendamo.
17 Ndipo ndinaika alonda oyang’anira inu, ndi kuti, Mverani mau a lipenga; koma anati, Sitidzamvera.
18 Chifukwa chake tamverani,amitunduinu, dziwani, msonkhano inu, chimene chili mwa iwo.
19 Tamva, dziko lapansi iwe; taona, Ine ndidzatengera choipa pa anthu awa, chipatso cha maganizo ao, pakuti sanamvere mau anga, kapena chilamulo changa, koma wachikana.
20 Lubaniandifumiranji ku Sheba, ndi nzimbe ku dziko lakutali? Nsembe zopsereza zanu sizindisekeretsa, nsembe zophera zanu sizindikondweretsa Ine.
21 Chifukwa chake atero Yehova, Taona, ndidzaikira anthuwa zophunthwitsa; ndipo atate ndi ana adzakhumudwa nazo pamodzi; munthu ndi mnzake adzatayika.
22 Yehova atero, Taona, mtundu wa anthu uchokera kumpoto; ndi mtundu waukulu udzaukitsidwa ku malekezero a dziko lapansi.
23 Agwira uta ndi nthungo; ali ankharwe, alibe chifundo; mau ao apokosera ngati nyanja, akwera pa akavalo; aguba monga anthu ofuna kumenyana nkhondo ndi iwe, mwana wamkazi waZiyoni.
24 Tamva ife mbiri yake; manja athu alefuka, yatigwira nkhawa ndi zowawa ngati za mkazi wobala.
25 Usatulukire kumunda, usayenda m’njira; pakuti lupanga la amaliwongo ndi mantha ali m’mbali zonse.
26 Iwe mwana wamkazi wa anthu anga, udziveke ndi chiguduli, ndi kumvimvinika m’phulusa; ulire maliro ngati a mwana wamwamuna wa yekha, kulira kowawa koposa; pakuti wakufunkha adzatifikira ife motidzidzimutsa.
27 Ndakuyesa iwe nsanja ndi linga mwa anthu anga, kuti udziwe ndi kuyesa njira yao.
28 Onse ali opikisana ndithu, ayendayenda ndi maugogodi; ndiwo mkuwa ndi chitsulo; onsewa achita movunda;
29 mvukuto yatenthedwa ndi moto; mtovu watha ndi moto wa ng’anjo; ayenga chabe; pakuti oipa sachotsedwa.
30 Anthu adzawatcha nthale yasiliva, pakuti Yehova wakana iwo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/6-5930f3b8ce7f427ff501a337ed07b27b.mp3?version_id=1068—